Mpandamachokero Anthology by Bonwell Rodgers
MPANDAMACHOKERO ANTHOLOGY By Bonwell Rodgers
- Page 2 and 3: Mawu Oyamba M’bukuli muli nthano
- Page 4 and 5: Mbalame Yodzimva M’nkhalango ina
- Page 6 and 7: “Mwayankhula bwino pamenepo a Nan
- Page 8 and 9: Osavula zigoba mwavalazo bwanji?”
- Page 10 and 11: Nkhandwe ya Mtima Wangati Kuseri kw
- Page 12 and 13: Galu Apusitsidwa ndi Chithunzithunz
- Page 14 and 15: Mkango Unatenga Zonse Tsiku lina Mk
- Page 16 and 17: Dokowe Apulumutsa Nkhandwe Tsiku li
- Page 18 and 19: Mpandamachokero Kalelo, pamudzi win
- Page 20 and 21: Kusamvana Pakati pa Munthu ndi Njok
- Page 22 and 23: Khoswe Wam’tauni ndi Khoswe Wakum
- Page 24 and 25: ukufuna kubwerera kumudzi nthawi yo
- Page 26 and 27: Monga malipiro a nyama ndatengayi,
- Page 28 and 29: Phunziro: Ndi anthu amatha amene am
- Page 30 and 31: wachita misala, ndipo anatenga ndod
- Page 32 and 33: chinaduka. Kenako anauza Mkangowo k
- Page 34 and 35: Kumachotseratu mbewu yoipa isanamer
- Page 36 and 37: mwamantha ndipo sankayandikira n’
- Page 38 and 39: Phokoso la Mapiri Tsiku lina anthu
- Page 40 and 41: Akalulu Akumana Ndi Mavuto Nthawi i
- Page 42 and 43: Ukakwera M’mwamba Usamatukwane Pa
- Page 44 and 45: Pansi pa Mtima Tsiku lina Gondwa an
- Page 46 and 47: Njoka Yopanda Pabwino Chaka china k
- Page 48 and 49: Ntchentche Yosimbwa Kalelo kunali b
- Page 50 and 51: Nkhandwe Ichezera Dokowe Kalekalelo
MPANDAMACHOKERO<br />
ANTHOLOGY<br />
By <strong>Bonwell</strong> <strong>Rodgers</strong>
Mawu Oyamba<br />
M’bukuli muli nthano za ana. Nthano zina ndi zoti<br />
zinalembedwa ndi akatswiri akale kwambiri ndipo<br />
zinamasuliridwa n’kukonzedwa mwina ndi mwina,<br />
pomwe zina ndi za kwathu konkuno ku Malawi.<br />
Nthanozi ndi zazifupi koma zosangalatsa. Wolemba<br />
bukuli anaona kuti anthu ambiri sakonda kuwerenga<br />
nkhani zazitali. Choncho analemba nthano zazifupi<br />
koma zomveka bwino. Nthanozi ndi zoti zikhoza<br />
kugwiritsidwa ntchito pophunzitsa kusukulu,<br />
powerengera ana komanso pocheza. Bukuli<br />
lingathandizenso ana kuphunzira ukadaulo wopinda<br />
komanso kuseweretsa mawu m’Chichewa.<br />
Kuwonjezera apo, nthano zake ndi zokhathamira ndi<br />
nsinjiro za chiyankhulo.<br />
The Series of <strong>Rodgers</strong> Bounty Books [RBB]<br />
Copyright © January 2015 <strong>by</strong> <strong>Bonwell</strong> <strong>Rodgers</strong>.<br />
All rights reserved. No part of this publication may be reproduced or transmitted in any form or <strong>by</strong> any means, electronical or<br />
mechanical, including photocopy, recording or any imformation storage and retrieval system, without permission in writing from the<br />
owner.<br />
Requests for permission should be mailed to: <strong>Bonwell</strong>rodgers91@gmail.com<br />
Phone: 0881813953, 0881831435<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
1
Nthano Zokhala ndi Maphunziro<br />
“Tikhoza kuphunzira zambiri ngakhale kuchokera kwa<br />
nyama zakutchire. Chilichonse chili ndi pokomera,<br />
kungoti umafunika kufufuza mosamala kuti upaone<br />
pokomerapo.”<br />
—Anatero Lewis Carrol m’buku lake lakuti, Alice’s<br />
Adventures in Wonderland<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
2
Mbalame Yodzimva<br />
M’nkhalango ina munali mbalame yokongola kwambiri<br />
yomwe inkadya moto chifukwa cha kuyerekedwa<br />
kwake. Dzina la mbalameyi linali Pikoko. Mbalameyi<br />
inali yaphunzo chifukwa inkanyoza zinzake zomwe<br />
zinali ndi nthenga zosaonetsa kugulu la anthu.<br />
Inalinso yodzimva komanso yodzikuza zedi. Tsiku lina<br />
mbalame zonse zitakhuta, zinapita pachitsime pomwe<br />
zinkakamwa madzi. Mbalamezi zinkafunika kufola<br />
pamzere kuti zikamwe madziwo. Ndiye chifukwa<br />
chodziona kukongola, mbalame ija yotchedwa Pikoko<br />
inangoyenda kupita kutsogolo n’kudutsa zinzake<br />
zonse zomwe zinafika mofulumira. Mbalameyi<br />
inkayenda monyang’wa ngati sipita kuchumbudzi, ili<br />
palasu palasu palasu mpaka inakafika kutsogolo<br />
kwenikweni. Anzake anaifunsa amvekere: “Chikatere?”<br />
A Pikoko pomva izi anayamba kulavula mwano.<br />
“Mulungutu enafe anatikondera! Kodi mumatichitira<br />
nsanje eti?”<br />
Mbalame zinzake zinadandaula kuti: “Chitsime<br />
n’chimodzi m’mudzi muno, aliyense ayenera<br />
kuchitiridwa mofanana kaya ali ndi nthenga zokongola<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
3
kapena ayi, chilungamo chiziyenda ngati madzi!”<br />
Koma mbalame ija inatuzula maso kwinaku<br />
ikutokosera m’mano ndipo kenako inageyanso<br />
chipongwe china cholama.<br />
“Kodi mbalame zosasamba zikudzatani kuno? . . . Inu<br />
a Khwangwala, ngati mumafuna kuchitiridwa zinthu<br />
mofanana ndi enafe ingopitani kumanda! Ndipo<br />
ndimadabwa kuti n’chifukwa chiyani nawonso manda<br />
samaona kuti enafe tili ndi nthenga zokongola?<br />
Tikazitambasula anthu amagwetsa zibwano zawo,<br />
kudabwa kumeneko!”<br />
Nang’omba atamva izi anatsutsa Pikoko. Kumenekotu<br />
ndi kuyankhula kwa ntudzu komanso kogudukira.<br />
Kukongoladi kwa mbalame n’kulinga utaiona<br />
itatsegula pakamwa! Ndikuuzeni pano mosapsatira<br />
mawu achikulire, kukongola kwa nthengaku<br />
sikungakupangitseni kukhala wanzeru! Enafe<br />
tinangoipa maonekedwewa, muntimamu si khalidwe<br />
lake. Komanso tili ndi chikondi chopangitsa munthu<br />
kuiwala kwawo!”<br />
Mbalame zina zonse zinagwedezera mitu<br />
povomerezana ndi a Nang’omba.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
4
“Mwayankhula bwino pamenepo a Nangomba!” Inatero<br />
Nthiwatiwa. A Nthiwatiwa sanadziwe kuti zimene<br />
anachitazo kunali kudzipalasira makala a moto,<br />
ukadziotche weniweni. Pa nthawiyi n’kuti Pikoko<br />
atapsa mtima, ukali ukutulukira mumphuno komanso<br />
m’makutu, kwinaku atafutukura mapiko ake pofuna<br />
kuwaonetsa anzakewo apo panagona kukongola<br />
kwake. Kenako inakoka mtsonyo ikuyangana a<br />
Nang’omba omwe anayandikana ndi a Nthiwatiwa.<br />
Ndiyeno inayamba kulavula chichewa chitalichitali<br />
chothiga ndi phunzo.<br />
“Inu a Nang’omba ndinu chibenga. Nanunso a<br />
Nthiwatiwa muli tiwa ngati nsungwi, zovala<br />
zinakuthawani kalekale. Kodi simunamve kuti<br />
munthu ukamafuna dzino lalikulu umafunika<br />
kuutumba mulomo waukulu woti uvindikirire dzinolo?<br />
Kutalika muli thobo, n’kumalephera kupeza zovala za<br />
msinkhu wanu. Mumabwerekana zovala ndi mwana<br />
wanu kapena? Mbalame zosasambanu mumatha<br />
mawu kwabasi. Kaya n’kusowa khobili logulira<br />
chinkhupule! Miyendo imeneyo ingapulumuke<br />
mutakumana ndi khwekhwe kapena chimvwapula?<br />
Mukamayenda mumangonunkha nkhwema<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
5
kunkhwapa, simutisanzitsa inu? Kapena mumafuna<br />
enafe tizichita nseru kuti chakudya m’malunjemu<br />
chizitibwerera kukhosi! Umbombo wamtundu wanji<br />
wofuna muzigalika nokha! Mukamayenda muli mimba<br />
tiyetiye, nthenga zili yaviyavi, n’kumangooneka ngati<br />
kamvuluvulu . . .”<br />
Chipongwe chimenechi chinawafikapo a Nthiwatiwa<br />
moti anayamba kuphulusika. Kenako anati:<br />
“N’chifukwa chiyani anthu omwe muli pabwino<br />
mumayankhula motumbwa?”<br />
Koma a Pikoko anati: “Pajatu chilungamo<br />
n’chipongwe! Kungoti enafe sitibisa mawu. Ena<br />
akamatizolowera timangowamasura!”<br />
Ndiyeno a Mkuta analowererapo n’kuuza a Pikoko<br />
kuti, “Nafenso tikumasureni lero. Khalidwe lanu<br />
limatinyansa, bolanso chimbudzi cha njovu kapena<br />
fungo la dzila lowola.”<br />
“Choka wouma mutu iwe!” Anatero a Pikoko.<br />
“Namalenga ndiye anandinikha kukongolaku. Ngati<br />
mumadziimba mlandu chifukwa cha kusaoneka bwino<br />
kwanuko, mukawasumire makolo anu! Kodi<br />
ndikanena chilungamo ndiye ndisanduke woipa?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
6
Osavula zigoba mwavalazo bwanji?”<br />
Mbalame zonse zinadzuma ndipo ina yomwe inkamwa<br />
madzi inatsamwa. Nthawi yomweyo Kadzidzi yemwe<br />
n’kuti maso ake ali psuu chifukwa chosala tulo, zikope<br />
zili thyo kuthyoka, anati: “A Pikokoo, palibetu<br />
wangwiro padziko lapansi pano. Taonani miyendo<br />
yanuyo!”<br />
Mbalame zonse zinafa nawo nseko ndipo zina<br />
zinangotsala pang’ono kukomoka chifukwa cha<br />
chikhakhali. Zinkaseka miyendo ya a Pikoko yomwe<br />
inali mbuu kutuwa ndipo inkangooneka ngati<br />
zotokosera m’mano. Chifukwa cha manyazi, a Pikoko<br />
anangosamukapo pachitsimepo, koma nyota<br />
itangalula kukhosi.<br />
Phunziro: Si bwino kukhala wodzikuza chifukwa<br />
ngakhale utakhala ndi luso umakhala ndi penapake<br />
pamene umalephera.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
7
Mafunso:<br />
1. N’chifukwa chiyani a Pikoko samafuna kukhala<br />
pamzere?<br />
2. Kodi n’chiyani chikusonyeza kuti a Pikoko<br />
anali wodzikuza?<br />
3. Kodi pakati pa kukongola ndi khalidwe<br />
labwino, chofunika kwambiri n’chiyani?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
8
Nkhandwe ya Mtima Wangati Kuseri kwa<br />
Mphika<br />
Kalekalelo Nkhandwe inapita kukamwa madzi padziwe<br />
lina lomwe linali pafupi ndi phiri. Itafika kumeneko<br />
inaima chakumtunda n’kuyamba kupha ludzu.<br />
Itamwaza maso inaona Nkhosa, nayonso ikumwa<br />
madzi kumunsi kwa dziwelo. Kenako inayamba<br />
kuganiza kuti, “Ndikhozatu kutsuka m’kamwa ndi<br />
kandiwo kameneka. Nditangopeza chifukwa chabwino,<br />
ndikhoza kukaonetsa zakuda ndithu.” Ndiyeno itadya<br />
mutu inayamba kuyankhula mwaukali kwa Nkhosayo<br />
kuti, “N’chifukwa chiyani ukudetsa madzi amene<br />
ndikumwa?” Nkhosayo inayankha kuti, “Ayi, si ine.<br />
Ngati madziwo akubwera akuda kumeneko, vuto si ine<br />
ayi. Nokhanso mukuona kuti madziwa akuchoka<br />
kumeneko n’kumabwera kuno.” Kenako Nkhandwe ija<br />
inati, “Watero, chabwino, nanga n’chifukwa chiyani<br />
unkanditukwana chaka chatha chija nditabwera<br />
kudzamwa madzi kuno?” Nkhosayo inayankhanso<br />
kuti, “Si inenso ameneyo, inetu ndili ndi miyezi isanu<br />
ndi umodzi wokha, moti nthawi imeneyo ndinali<br />
ndisanabadwe.” Itamva zimenezi, Nkhandweyo<br />
inakwiya kwambiri ndipo inati, “Ndilibe nazo ntchito<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
9
zimenezo, ngati sunali iweyo ndiye kuti anali bambo<br />
ako.” Itangonena zimenezi inathamangira kunali<br />
Nkhosa kuja n’kuimbwandira, ndipo kenako inaidya.<br />
Phunziro: Munthu woipa sasowa chonamizira.<br />
Amachita chilichonse kuti akwaniritse cholinga chake<br />
ngakhale kupha munthu kumene.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi m’nthanoyi ndi nyama iti imene ili yoipa<br />
mtima? N’chifukwa chiyani mwayankha choncho?<br />
2. N’chifukwa chiyani mutu wa nkhaniyi<br />
ukuyerekeza mtima wa nkhandwe ndi kuseri kwa<br />
mphika?<br />
3. Perekani chitsanzo cha munthu woipa mtima<br />
yemwe anachitira mnzake zankhanza, ngakhale<br />
kuti mnzakeyo anali wosalakwa.<br />
4. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
10
Galu Apusitsidwa ndi Chithunzithunzi<br />
Tsiku lina Galu anatola nyama ndipo anaipana<br />
n’kumapita nayo kwawo kuti akaidye mwamtendere.<br />
Koma kuti akafike kwawo, ankafunika kuwoloka<br />
mtsinje wina, ndipo kuti awoloke mtsinjewo<br />
ankayenera kudutsa pamlatho waung’ono. Galuyo<br />
atayamba kuwoloka kudzera pamlathowo, anaona kuti<br />
m’madzi mukuoneka chithunzithunzi cha Galu<br />
atanyamula nyama kukamwa kwake. Ataona zimenezi,<br />
anaganiza kuti ameneyo ndi Galu wina. Chifukwa<br />
chosakhutira ndi nyama yomwe anali nayo, Galuyo<br />
anaganiza zolanda nyamayo kuti ikhalenso yake.<br />
Ndiyeno mwamphamvu, analumphira m’madzi muja,<br />
kuti khuvuu! Koma atangotsegula kukamwa kwake,<br />
nyama ananyamula ija inagwera m’madzi ndipo<br />
anaisakasaka koma sanaipeze. Pamenepo m’pamene<br />
anazindikira kuti Galu amaoneka mumtsinje uja<br />
chinali chithunzithunzi chake.<br />
Phunziro: Musalole kutaya zonse zomwe muli nazo kuti<br />
mupeze zinthu zomwe mukuganiza kuti mukhoza<br />
kuzipeza. Kumakhutira ndi zomwe muli nazo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
11
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Galuyu ankafunanso<br />
kulanda nyama ya Galu amene ankamuona<br />
m’madzi, kodi anali ndi njala?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti Galu angachitedi<br />
zimenezi? N’chifukwa chiyani mwayankha<br />
choncho?<br />
3. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
12
Mkango Unatenga Zonse<br />
Tsiku lina Mkango unapita kosaka limodzi ndi Agalu<br />
am’tchire atatu. Nyama zimenezi zinasaka, kusaka,<br />
kenako n’kusaka koma sizinagwire kanthu. Ndiyeno<br />
mwamwayi, nyamazi zinasokolotsa Mphalapala ndipo<br />
posakhalitsa zinaigwira n’kuipha. Zitatere, Agalu<br />
am’tchirewo anayamba kunena kuti, “M’pofunika kuti<br />
tonse tigawane nyamayi mofanana.” Koma Mkango<br />
unabangula n’kuuza Agaluwo kuti, “Dulani nyamayi<br />
panayi!” Agalu aja anamveradi zimenezo ndipo<br />
anasenda nyamayo n’kuidula panayi. Kenako Mkango<br />
uja unaima patsogolo pa nyamayo n’kuyamba<br />
kulongosola za kagawidwe kake. Unati: “Mbali<br />
yoyambayi ikhala yanga chifukwa ndine Mfumu ya<br />
Zinyama zonse m’nkhalango muno. Mbali yachiwiriyi<br />
ikhalanso yanga chifukwa ndine ndinayambitsa<br />
ulenjewu. Pomwe mbali yachitatuyi ikhalanso yanga<br />
chifukwa ndinathamangitsa nawo nyamayi. Koma<br />
ponena za mbali yotsalayo, amene ali wolimba mtima<br />
ayerekeze kuigwira aone . . . . ” Atamva zimenezi,<br />
Agalu am’tchirewo anadzuma chapansipansi ndipo<br />
kenako ananyamuka n’kumapita, kwinaku atapanira<br />
michira yawo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
13
Phunziro: Mukhoza kuthandiza anthu amphamvu<br />
kuchita zinazake, koma simungadye nawo zimene<br />
angapeze.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Agalu am’tchire ankathawa<br />
atapanira michira?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti Agaluwo ankayenera<br />
kudya nawo nyamayo? N’chifukwa chiyani<br />
mukutero?<br />
3. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
14
Dokowe Apulumutsa Nkhandwe<br />
Tsiku lina Nkhandwe inali ndi njala zedi ndipo<br />
inagwira nyama n’kuyamba kuipwepweta<br />
mwankhanza. Koma mwatsoka fupa linaima pammero,<br />
moti inkalephera kulimeza. Nkhandweyo inayamba<br />
kumva ululu woopsa ndipo inkabuula kwinaku<br />
ikupempha nyama zina kuti aithandize. Koma<br />
chifukwa cha khalidwe lake la umadyera mphoto,<br />
nyama zina zinkachita mantha, moti palibe inalimba<br />
mtima kuithandiza. Kenako Nkhandweyo inayamba<br />
kunyengerera aliyense amene inkakumana naye<br />
n’cholinga choti aipulumutse. Inkati, “Ndikupatsani<br />
chilichonse chimene mukufuna ngati mutandichotsa<br />
fupali kukhosiku.” Mwamwayi, Dokowe anavomera<br />
kuti ayesa kuchotsa fupalo, ndipo anaiuza kuti igone<br />
pansi n’kutsegula kukamwa kwake. Dokoweyo<br />
anapisa kukhosi kwa Nkhandweyo ndi mulomo wake<br />
ndipo khosi lake lonse lalitalilo linalowa m’kamwa<br />
mwa Nkhandweyo. Dokoweyo anakwanitsadi kuchotsa<br />
fupalo ndipo Nkhandweyo inayamba kupeza bwino.<br />
Ndiyeno Dokowe anauza Nkhandweyo kuti, “Tsopano<br />
popeza ndachotsa fupali, ndininkhenitu zimene<br />
munalonjeza zija. Pajatu lonjezo linadulitsa mutu wa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
15
nkhuku!” Itamva zimenezi, Nkhandweyo inamwetulira<br />
n’kuonetsa mano ake, ndipo kenako inati,<br />
“Muziyamika a Dokowe. Inuyotu munalowetsa mutu<br />
wanu m’kamwa mwanga n’kuutulutsamo uli<br />
bwinobwino, popanda vuto lililonse. Ndiye mukuti<br />
mukufuna ndikupatseninso mphoto ina kuposa<br />
imeneyo?”<br />
Phunziro: Munthu wadyera sayamika.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />
Dokowe anathandiza Nkhandwe?<br />
2. N’chifukwa chiyani Dokowe anauza Nkhandwe<br />
kuti imupatse zimene inalonjeza?<br />
3. Kodi mukuganiza kuti Nkhandwe inaperekadi<br />
mphoto kwa Dokowe? N’chifukwa chiyani<br />
mukutero?<br />
4. Tiyerekeze kuti Nkhandweyo inakana kupereka<br />
mphoto kwa Dokowe, kodi tinganene kuti<br />
inalakwa?<br />
5. N’chifukwa chiyani tiyenera kumachitadi<br />
zimene talonjeza?<br />
6. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
16
<strong>Mpandamachokero</strong><br />
Kalelo, pamudzi wina panali mkamwini wina yemwe<br />
ankasakasaka chifukwa chopitira kwawo. Anthu a<br />
pamudzipo ankakhala naye bwino zedi. Koma kenako<br />
munthuyu anatopa ndi ulemu, ndipo anayamba<br />
kusakasaka chifukwa chochokera pakhomopo. Ndiye<br />
tsiku lina, ana ankaphika masanje ndipo mkamwiniyo<br />
anapita pomwe anawo anakoleza moto wawo<br />
n’kuukodzera. Anawo anayamba kulira ngati kuti wina<br />
wawatsina, moti akuluakulu a pamudzipo anatuluka<br />
m’nyumba kuti akaone chomwe chachitika. Atafunsa<br />
anawo kuti chachitika n’chiyani, anaulula kuti<br />
mkamwiniyo wawazimitsira moto wawo komanso kuti<br />
anachita kuukodzera. Akuluakuluwo anakhumudwa<br />
kwambiri ndipo anapita kunyumba kwa mkuluyo kuti<br />
akamufunse za nkhaniyo. Atafika, mkamwiniyo<br />
anawalandira n’kuwalowetsa m’nyumba. Anthuwo<br />
anapepesa chifukwa chobwera mwadzidzidzi, koma<br />
mkamwiniyo anati, “Ayi, mwafika mwatha.” Ndiye<br />
kenako anawauza kuti, “Tikupunguleni mpweya!”<br />
Zitatero anthu a pamudzipo anayamba kuyala nkhani<br />
yonse. Koma mkamwiniyo atamva zimene anthuwo<br />
ananena, anakwiya kwambiri ndipo anati: “Zoona<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
17
mmene ndakuliramu ndingakodzere moto wa ana?<br />
Anthu inutu simukundifuna pamudzi pano. Basi<br />
ndikupita kwathu.” Kenako anamanga nsanza zake<br />
pachitenje, n’kunyamuka kumapita kwawo.<br />
Phunziro: Anthu ena akatopa kukhala pamalo,<br />
amachita kusakasaka chifukwa chochokera.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi vuto la mkamwiniyu linali chiyani?<br />
2. Kodi pali umboni wanji wosonyeza kuti anthu a<br />
pamudziwu anali abwino?<br />
3. Kodi mukuganiza kuti mkamwiniyo<br />
ankatanthauza chiyani pamene ananena kuti,<br />
“tikupunguleni mpweya”?<br />
4. Kodi mwambi wakuti, “mpandamachokero<br />
adakodzera moto wa ana” unayamba bwanji?<br />
5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
18
Kusamvana Pakati pa Munthu ndi Njoka<br />
Mwana wa Mlimi wina anaponda mchira wa Njoka<br />
mwangozi, ndipo Njokayo inalusa n’kumugagada, moti<br />
anafera pomwepo. Bambo a mwanayo atamva zimenezi<br />
anakwiya zedi, ndipo ananyamula nkhwangwa<br />
n’kuyamba kuthamangitsa Njokayo. Ataipeza<br />
anaponya nkhwangwayo ndipo anaidula mchira.<br />
Zimenezi zinachititsa kuti njokayo ikwiye zedi, moti<br />
inaganiza zokhaulitsa mlimiyo. Inanyamuka n’kupita<br />
m’khola la mlimiyo n’kukaluma ng’ombe zonse, moti<br />
inasiya mlimiyo manja ali m’khosi, ng’ombe zake zonse<br />
zitafa. Koma kenako mlimiyo anaona kuti kubwezera<br />
sikuthandiza, ndipo anaganiza zokambirana ndi<br />
Njokayo kuti akhazikitse mtendere. Choncho tsiku lina<br />
Mlimiyo anauyamba ulendo wopita kwa Njokayo<br />
atatenga kaphoso ka chakudya komanso uchi, ndipo<br />
atafika anaika zinthuzo pauna wa Njoka n’kuodira.<br />
Njoka itatuluka, Mlimiyo anati, “M’bale wanga njoka,<br />
tiye tiiwale zakale. Ndikuona kuti n’zomveka kuti<br />
unalanga mwana wanga atakuchitira chipongwe.<br />
Komanso n’zomveka kuti unapha ng’ombe zanga<br />
utakwiya chifukwa chodulidwa mchira. Komabe,<br />
popeza ndine bambo wa mwana unapha uja,<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
19
sindinalakwe kukudula mchira chifukwa monga<br />
ukudziwira, imfa ya mwana imakhala yowawa<br />
kwambiri. Ndiye popeza aliyense wakhutira ndi zimene<br />
wachitira mnzake, tiye tiiwale zakale n’kuyambiranso<br />
kugwirizana.” Pamenepo Njokayo inati: “Ayi,<br />
sindikufuna. Pita nazo uko zinthu zakozo! Ndikudziwa<br />
kuti sungaiwale imfa ya mwana wako, komanso ineyo<br />
sindingaiwale za mchira wanga, womwe iweyo<br />
unaudula mopanda chisoni.”<br />
Phunziro: Nthawi zina zimatheka kukhululukira<br />
munthu, koma osaiwala zomwe anakuchitira.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Mlimi anatenga chakudya<br />
komanso uchi popita kukakumana ndi Njoka?<br />
2. N’chifukwa chiyani Njoka inakana kulandira<br />
mphatso zomwe Mlimiyo anapititsa?<br />
3. Kodi zimene Njokayo inachita ndi zabwino?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
20
Khoswe Wam’tauni ndi Khoswe<br />
Wakumudzi<br />
Kalekalelo Khoswe Wam’tauni anapita kukacheza kwa<br />
msuweni wake, yemwe ankakhala kumudzi. Khoswe<br />
Wakumudziyo anasangalala kwambiri ndi zimenezi<br />
moti anamulandira ndi manja awiri mnzakeyo.<br />
Ngakhale kuti analibe zinthu zambiri, Khoswe<br />
Wakumudziyo anayesetsa kukonzera mnzakeyo<br />
chakudya chabwino. Mwachidule tingoti anamupatsa<br />
zonse zomwe akanakwanitsa. Anamupatsa nyemba,<br />
nyama, mabanzi komanso mtedza. Ndiyeno Khoswe<br />
Wam’tauni uja anasolola mphuno yake n’kuyamba<br />
kununkhiza mosonyeza kuti chakudyacho<br />
chikumunyansa, ndipo kenako anati: “Asuweni<br />
sindimakumvetsani. Kodi mumakwanitsa bwanji<br />
kudya chakudya ngati chimenechi? Koma m’pomveka,<br />
kunoko n’kotsalira kwambiri moti simungakwanitse<br />
kupeza zakudya zonona komanso zabwinozabwino<br />
zomwe zimapezeka m’tauni. Tiyeni tipite kwathu<br />
ndikakuonetseni kukoma kwa moyo. Mukakangokhala<br />
sabata imodzi, mukaona kuti moyo womwe<br />
mukukhala kunowu ndi wofanana ndi kukhala<br />
kundende.” Nthawi yomweyo makoswe awiriwo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
21
anauyamba ulendo wopita m’tauni ndipo anafika<br />
usiku kwambiri kunyumba kwa Khoswe Wam’tauni<br />
uja. Kenako Khoswe Wam’tauniyo anati: “Ukuoneka<br />
kuti waweyeseka ndi ulendo, bwanji ndikupatseko<br />
zokhwasulakhwasula? Tabwera kuno!” Kenako<br />
anagwira mnzakeyo dzanja n’kuyamba kumukoka<br />
kupita naye kuchipinda chodyera. Kumeneko anapeza<br />
kuli zinthu zambiri zomwe zinatsala patebulo moti<br />
sanachedwenso ayi, koma kuyamba kudya makeke<br />
komanso zakudya zina zokhetsa dovu, zomwe<br />
anazipeza m’chipindacho. Koma mwadzidzidzi,<br />
anamva agalu akuuwa. Ndiyeno Khoswe Wakumudzi<br />
anafunsa kuti, “Kodi chimenecho n’chiyani?”<br />
Mnzakeyo anayankha kuti, “Aa, usaope. Amenewo ndi<br />
agalu a m’nyumba muno.” Ndiyeno Khoswe<br />
Wakumudziyo anati, “Wati ndisaope? Kwathu<br />
ndimadya mwamtenderetu ine, moti phokoso limenelo<br />
silikundisangalatsa.” Posakhalitsa chitseko<br />
chinatseguka mwamphamvu ndipo Agalu akuluakulu<br />
awiri anatulukira. Makoswe awiriwo atangoona<br />
agaluwo, anayamba kuthawa pofuna kupulumutsa<br />
miyoyo wawo. Kenako Khoswe Wakumudzi anati,<br />
“Msuweni, ine ndikupita kwathu.” Khoswe<br />
Wam’tauniyo anafunsa mnzakeyo kuti, “Bwanji,<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
22
ukufuna kubwerera kumudzi nthawi yomweyi?” Koma<br />
Khoswe Wakumudziyo anati, “Inde, ndikupita. Bola<br />
ndizikadya nyemba komanso mabanzi ndili<br />
pamtendere, kusiyana n’kumadya makeke komanso<br />
zinthu zonona ndili ndi mantha.”<br />
Phunziro: “Ndi bwino kumadya chisoso pali mtendere,<br />
kusiyana ndi kumadya nyama uli ndi mantha.”<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Khoswe Wakumudzi<br />
anapita m’tauni?<br />
2. N’chifukwa chiyani khosweyu anabwerera<br />
kumudzi?<br />
3. Kodi pali kusiyana kotani pakati pa Khoswe<br />
Wakumudzi ndi Khoswe Wam’tauni?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
23
Nkhadwe Inapusitsa Khwangwala<br />
Tsiku lina Nkhandwe inaona Khwangwala akuuluka.<br />
Khwangwalayo anali atapana nyama kukamwa kwake.<br />
Posakhalitsa Khwangwalayo anatera mumtengo wina<br />
ndipo Nkhandwe inaganiza kuti, “Ndikhozatu<br />
kumuyeretsa m’maso ameneyu.” Kenako inanyamuka<br />
n’kupita pafupi ndi mtengo anatera Khwangwala uja<br />
n’kunena kuti, “Muli bwanji Mayi Khwangwala?<br />
Mukuonekatu bwino lero. Mwatchena suti yokongola<br />
zedi, yomwenso ikugwirizana ndi kakolala koyera<br />
komwe kali m’khosi mwanuko. Mukuonekanso kuti<br />
mukhoza kuimba mwanthetemya kuposa mbalame<br />
zina zonse. Ndiponsotu mawu anu amandisangalatsa<br />
zedi, moti mungachite bwino mutandiimbira kanyimbo<br />
mumakonda kuimba kaja, . . . kamene kaja.<br />
Mukangochita zimenezi, nthawi zonse ndizikupatsani<br />
moni waulemu monga Mfumukazi ya Mbalame zonse.”<br />
Khwangwalayo atamva zimenezi anapusitsika ndipo<br />
anatukula mutu wake n’kuyamba kuimba, amvekere<br />
khwaa! khwaa! khwaa! Koma atangochita zimenezi,<br />
nyama inali kukamwa kwake ija inagwera pansi ndipo<br />
Nkhandwe ija inatola n’kunena kuti, “Zikomo<br />
kwambiri mayi. Zimene ndimafuna ndi zimenezi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
24
Monga malipiro a nyama ndatengayi, ndikupatsani<br />
malangizo oti adzakuthandizeni m’tsogolo.<br />
Mukadzaona munthu akukutamandani pa chifukwa<br />
chosadziwika bwino, mudzadziwe kuti akufuna<br />
kukupondani.”<br />
Phunziro: Osamakhulupirira anthu achinyengo.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi ndi ndani amene anali tambwali pakati pa<br />
Nkhandwe ndi Khwangwala?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inapempha<br />
Khwangwala kuti amuimbire nyimbo?<br />
3. Nanga n’chiyani chimene chinakopa<br />
Khwangwala kuti aimbedi nyimboyo?<br />
4. Kodi n’zoona kuti Khwangwala analidi<br />
mbalame yokongola komanso yodziwa kuimba?<br />
5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
25
Mkango Udwala Mwakayakaya<br />
Nthawi ina Mkango unakalamba kwambiri moti<br />
unayamba kudwala mwakayakaya pakhomo la phanga<br />
lake. Mkangowo unkangokhalira kubuula tsiku lonse<br />
ndiponso unkavutika kupuma. Nyama zina za<br />
m’nkhalango zinabwera kudzazonda matendawo koma<br />
popeza Mkango ndi nyama yoopsa, zinaima chapatali<br />
ndithu. Koma zitaona kuti Mkangowo ulibenso<br />
mphamvu komanso kuti moyo wake wangotsala madzi<br />
amodzi, zinayamba kuyandikira pang’onopang’ono.<br />
Zina mwa nyamazo zinayamba kuganiza kuti,<br />
“Tsopano nthawi yakwana yoti tibwezere zonse zimene<br />
Mkango unatichitira.” Ndiyeno Nguluwe inathamanga<br />
n’kukagunda Mkangowo. Kenako Njati nayonso<br />
inadzambatuka n’kukaubaya ndi nyanga zake. Koma<br />
palibe chimene Mkangowo unachita, unangogona<br />
pansi kwala! Choncho, Bulu ataona kuti Mkango<br />
sungachite kanthu, anapita pafupi ndi Mkangowo<br />
n’kuyamba kuvina kwinaku akugwedezera mchira<br />
wake, ndipo kenako anamenya Mkangowo ndi<br />
miyendo yake yakumbuyo. Mkangowo utaona zimenezi<br />
unalira modandaula kuti, “Apa ndiye ndifa kawiri<br />
ndithu. Zoona kumenyedwa ndi ana omwe?”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
26
Phunziro: Ndi anthu amatha amene amalimbana ndi<br />
munthu wamphamvu akamatsirizika.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani nyamazi zinkayandikira<br />
pang’onopang’ono?<br />
2. N’chifukwa chiyani nyama zina zinaukira<br />
Mkango?<br />
3. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Bulu<br />
anapita komalizira?<br />
4. Kodi kubwezera n’kulakwa?<br />
5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
27
Bulu Komanso Galu<br />
Tsiku lina Mlimi anapita kukaona ana komanso ziweto<br />
zake. Pakati pa nyamazi panali Bulu. Ndiye pamene<br />
Mlimiyo ankapita kumeneku, n’kuti ali limodzi ndi<br />
Galu wake yemwe ankamukonda kwambiri. Galuyo<br />
ankadumphadumpha n’kumanyambita komanso<br />
kugwira mkono wa Mlimiyo. Kenako Mlimiyo anapisa<br />
m’thumba n’kutenga chakudya n’kupatsa Galuyo,<br />
ndipo kenako anakhala pansi n’kuyamba kupereka<br />
malangizo kwa ana ake. Ndiyeno Galuyo analumphira<br />
pamiyendo pa Mlimiyo ndipo Mlimiyo anayamba<br />
kumusisita. Bulu uja ataona zimenezi anasilira<br />
kwambiri moti anadula chingwe chimene<br />
anamumanga nacho n’kuthamangira kwa Mlimiyo kuti<br />
nayenso akachite chimodzimodzi. Mlimiyo ataona<br />
zimenezi anayamba kuseka ndipo Buluyo ankaganiza<br />
kuti zimene akuchitazo zikumusangalatsa. Ndiye<br />
kenako anaganiza zoti alumphire pamiyendo pa<br />
Mlimiyo n’cholinga choti nayenso amusisite. Koma<br />
chifukwa cha kutalika, Buluyo sanakwanepo, moti<br />
miyendo yake inagwira m’mapewa mwa Mlimiyo. Ana a<br />
Mlimiyo ataona zimenezi anaganiza kuti Buluyo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
28
wachita misala, ndipo anatenga ndodo n’kuyamba<br />
kumuumbudza.<br />
Phunziro: Osamangotengera zilizonse zimene ena<br />
akuchita.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Bulu anaganiza zotengera<br />
zochita za Galu?<br />
2. Kodi Buluyo anakumana ndi zotani? Nanga<br />
n’chifukwa chiyani anakumana ndi zimenezo?<br />
3. Kodi n’kulakwa kumangotengera zochita za<br />
ena, bola ngati tikuona kuti zikuwayendera bwino?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
29
Khoswe Apulumutsa Mkango<br />
Tsiku lina Mkango ukugona, Khoswe anayamba<br />
kuukwerakwera. Zimenezi zinachititsa kuti Mkangowo<br />
udzidzimuke ndipo unagwira Khosweyo n’kutsegula<br />
kamwa lake kuti ungomuponyera m’kamwa<br />
n’kumutafuna. Koma Khosweyo anakuwa n’kuuza<br />
Mkangowo kuti, “Pepani Mfumu yanga,<br />
ndikhululukireni chonde! Ndimvereni chisoni, ndinetu<br />
mwana wamasiye! Mutandisiya wamoyo kano kokha,<br />
ndikhoza kudzakupulumutsani m’tsogolo!” Mkango<br />
utamva zimenezi unafa nalo phwete ndipo unati,<br />
“Usandiseketse m’kamwa, zoona iweyo kuchepa<br />
kumeneku ungandipulumutse?” Posakhulupirira<br />
zimenezi, Mkangowo unamusiyadi Khosweyo. Ndiyeno<br />
patapita nthawi, Mkango uja unagwidwa pamsampha,<br />
ndipo alenje atauona anaganiza zounyamula n’kupita<br />
nawo kwa mfumu yawo. Kenako anaugwira<br />
n’kuukwidzinga pamtengo n’kupita kukasakasaka<br />
ngolo yoti adzaunyamulire. Alenje aja atangochoka,<br />
Khoswe uja anadutsa pafupi ndi pomwe panali<br />
Mkango uja. Ataona mmene Mkangowo<br />
unkandandaulira, anapita pomwepo n’kuchecheta<br />
chingwe chomwe anaumangira chija, ndipo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
30
chinaduka. Kenako anauza Mkangowo kuti, “Si paja<br />
ndinakuuzani kuti ndikhoza kudzakupulumutsani!<br />
Mwaonatu, osamachepetsa kolemera.” Kenako<br />
ananyamuka n’kumapita.<br />
Phunziro: Nthawi zina anthu onyozeka ndi amene<br />
amathandiza kwambiri.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Mkango unasiya Khoswe<br />
kuti apite?<br />
2. Kodi Khoswe anathandiza bwanji Mkango?<br />
Nanga n’chifukwa chiyani anauthandiza?<br />
3. Pakati pa Khoswe ndi Mkango, kodi<br />
mukuganiza kuti ndi nyama iti imene<br />
inaphunzirapo kenakake?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
31
Namzeze Achenjeza Mbalame Zina<br />
Nthawi ina Mlimi anapita kukafesa mbewu ya chamba<br />
m’munda wina womwe Mbalame zinkakonda kukatola<br />
zakudya zake. Ndiye Mbalame ina yotchedwa Namzeze<br />
itaona zimenezi, inayamba kuchenjeza mbalame<br />
zinzake zomwe zinkatola zakudya m’mundawo. Inati,<br />
“Samalani ndi munthu uyo!” Mbalame zinazo<br />
zinamufunsa kuti, “Chifukwa? Kodi zimene akuchitazo<br />
ife zikutikhudza?” Iye anayankha kuti, “Munthuyu<br />
akufesa mbewu yoipa. Musayerekeze kusiya nthangala<br />
ngakhale imodzi ya mbewu zimenezi. Mukapanda<br />
kutero, mudzaona zakuda!” Mbalamezo zinkaona kuti<br />
zimene Namzeze ankakambazo ndi za kuntchini<br />
kwadzaza, moti sizinatsatire malangizowo. Koma<br />
patapita nthawi, mbewuzo zinayamba kukula ndipo<br />
mbalamezo zinayamba kuthothola masamba ake<br />
n’kumakamangira zisa. Pamene mbewu zija zinkacha,<br />
mbalame zosamverazo zinagwidwa zili m’zisa<br />
zopangidwa ndi masamba a chamba, omwe zinatenga<br />
m’munda uja. Mbalame zambiri zinasokonezeka ndi<br />
tsokali ndipo sizinkadziwa chifukwa chimene<br />
munthuyo ankatengera zisa zawo. Ndiyeno Namzeze<br />
anaziuza kuti, “Ndinakuuzani chiyani ine?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
32
Kumachotseratu mbewu yoipa isanamere! Mtsinje wa<br />
tinkanenatu unathera mu si izi.”<br />
Phunziro: Kumachotsa mbewu yoipa isanamere, apo<br />
ayi m’tsogolo imadzabweretsa mavuto.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mbewu yoipa imene namzeze ankanena<br />
inali chiyani? N’chifukwa chiyani mukutero?<br />
2. Kodi namzeze anauza mbalame zinzake kuti<br />
zichite chiyani?<br />
3. N’chifukwa chiyani Mlimiyo ankatenga zisa za<br />
mbalamezo?<br />
4. Kodi mungapereke zitsanzo za zinthu zina<br />
zoipa zimene ngati titazilekerera zikhoza<br />
kutibweretsera mavuto?<br />
5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
33
Achule Afuna Mfumu<br />
Achule ankakhala mosangalala m’dambo lina<br />
lokongola kwambiri. Nthawi zonse ankangokhalira<br />
kusewera. Ankati akadzuka m’mawa, ankayamba<br />
kuwothera dzuwa komanso kudya, ndipo akamva<br />
kutentha, ankakwera pamwala n’kudziponya m’madzi<br />
kuti mphavaa! Ankakhala kukhosi kuli mbee ndipo<br />
palibe chimene chinkawavutitsa. Komatu ukakhala<br />
pabwino, poipa pamakuitana. N’kupita kwa nthawi<br />
Achulewa anayamba kuona kuti moyo umenewu si<br />
wabwino, moti ankafuna atakhala ndi mfumu<br />
komanso malamulo abwino oti aziyendera. Choncho<br />
anaganiza zokapempha kwa Mulungu kuti awapatse<br />
mfumu yoti iziwalamulira. Iwo anati, “Mulungu wathu<br />
wamkulu, titumizireni mfumu yoti izitilamulira<br />
komanso kutipatsa malamulo oti tiziyendera.”<br />
Mulungu atamva zimene Achulewo ananena, anaseka<br />
ndipo anagwetsa chipika chachikulu chomwe<br />
chinagwera m’dziwe lomwe linali m’dambo lija.<br />
Achulewo anachita mantha kwambiri chifukwa cha<br />
phokoso lomwe linamveka pamene chipikacho<br />
chinkagwera m’madzi, moti onse anathawa n’kupita<br />
kumtunda. Kwa masiku ambiri, Achulewo ankakhala<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
34
mwamantha ndipo sankayandikira n’komwe chinthu<br />
choopsa chomwe chinagwera m’madzicho. Koma<br />
patapita nthawi, achulewo anaona kuti chinthucho<br />
sichikutakataka. Ndiyeno Achule ena olimba mtima<br />
anapita pafupi ndi chipika chija, moti ena analimba<br />
mtima n’kuchigwira. Komabe, chipikacho<br />
sichinasunthe. Kenako Chule wina, yemwe<br />
ankadziwika kuti ndi wolimba mtima kwambiri,<br />
analumphira pamwamba pachipikacho n’kuyamba<br />
kuvina, ndipo Achule enanso anayamba kuchita<br />
zomwezo. Izi zitachitika, Achulewo anatha mantha<br />
ndipo anayambanso kukhala monga mmene<br />
ankakhalira kale. Anaiwaliratu zoti Mulungu<br />
anawagwetsera chipika, chomwe chinali ngati mfumu<br />
yawo. Achulewo anayamba kuona kuti mfumuyi ndi<br />
yatulo ndiponso kuti ndi yosawayenera, moti<br />
anaganiza zopitanso kwa Mulungu kuti<br />
akapemphenso mfumu ina. Anati, “Tikufuna mfumu<br />
yeniyeni yoti izitilamulira, osati yomwe ikungoliza<br />
mkononoyi!” Zimenezi zinachititsa kuti Mulungu<br />
akwiye ndipo anatumiza Dokowe. Dokoweyo<br />
anayamba kujompha achulewo n’kumawadya.<br />
Achulewo ataona zimenezi, anachita mantha zedi moti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
35
anayamba kulirira Mulungu kuti awachotsere<br />
chilombocho, koma munali m’mbuyo mwa alendo.<br />
Phunziro: Ndibwino kukhala popanda mfumu<br />
n’kumakhala bwinobwino kusiyana ndi kukhala nayo,<br />
koma n’kukhala yankhanza.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />
Mulungu anatumiza chipika kwa Achule aja,<br />
m’malo mowapatsa mfumu yeniyeni?<br />
2. N’chifukwa chiyani achule anapitanso<br />
kukapempha mfumu ina?<br />
3. Kodi zangati zimene zinachitikira achulewa<br />
zimachitikanso masiku ano?<br />
4. N’chifukwa chiyani Mulungu anawakwiyira?<br />
5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
36
Phokoso la Mapiri<br />
Tsiku lina anthu a m’mudzi wina anayamba kumva<br />
phokoso loopsa lomwe linkamveka kuchokera<br />
m’Mapiri ena omwe anali pafupi ndi kwawo. Anthuwa<br />
ankaganiza kuti Mapiriwo akubereka ana. M’Mapiriwo<br />
munkatuluka chiutsi, nthaka inkangoti teketeke,<br />
mitengo inkangogwa komanso miyala inkangosweka.<br />
Iwo ankaona kuti pakhoza kuchitika chinachake<br />
choopsa. Anthuwo anasonkhana pamodzi kuti aone<br />
chomwe chitachitike. Anadikira, kudikira n’kudikira,<br />
koma palibe chinachitika. Kenako panachitikanso<br />
chivomerezi china champhamvu kwambiri moti<br />
nthaka inang’ambika pambali pa phiri lina. Anthuwo<br />
anayamba kuyang’ana mwachidwi m’phangalo ndipo<br />
anapitirizabe kudikira. Kenako anangoona kakhoswe<br />
kakang’ono kakuchokera m’phangalo. Kakhosweko<br />
kankapukuta mutu wake ndi timiyendo take<br />
tating’ono. Kenako kanatuluka n’kumalowera kumene<br />
kunali anthu aja. Kungochokera nthawi imeneyo<br />
anthuwo anayamba kunena kuti, “Pakakhala<br />
chiphokoso chachikulu, zotsatira zake zimakhala<br />
zogwetsa mphwayi.” Ndipo ena ankati, “N’chifukwa<br />
chaketu anthu a kum’mawa amanena kuti, ‘Chidebe<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
37
chopanda kanthu chimapanga phokoso kwambiri.’<br />
Mpake kuti ena amaganiza kuti, ‘anthu omwe<br />
sayankhulayankhula ndi amene amaganiza<br />
mwaphokoso zedi!”<br />
Phunziro: Nthawi zina anthu amene amalongolola<br />
kwambiri sachita zanzeru.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Anthu ankaganiza kuti chichitike<br />
n’chiyani?<br />
2. Kodi zimene Anthuwo ankayembekezera<br />
zinachitikadi?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
38
Akalulu Akumana Ndi Mavuto<br />
Nthawi inayake Akalulu ankazunzidwa ndi zilombo<br />
zina zosadziwika bwinobwino moti ankasowa<br />
kothawira. Zimenezi zinachititsa kuti akangoona<br />
nyama iliyonse azithawa n’kukabisala. Akaluluwa<br />
anafika potopa ndi zimenezi moti tsiku lina anaganiza<br />
zokangodziponya m’madzi n’kufa. Ndiye ataona Njati<br />
zikuthamanga, Akaluluwo anathawira kudziwe lina<br />
kuti akangodziponya m’madzi n’kulekana nawo moyo<br />
wokhala mwamantha. Ndiye atayandikira dziwelo,<br />
anadzidzimutsa Achule ena omwe ankaothera dzuwa<br />
ndipo nthawi yomweyo Achulewo anadziponya<br />
m’madzi. Kalulu wina ataona zimenezo anati, “Aa!<br />
akuluakulu, mavuto amene tili nawo ifewa, bola.<br />
Taonani anzathuwa! Ndaphunzirapo kanthu.<br />
Ukamakumana ndi mavuto, kumakumbukira kuti pali<br />
ena omwe akukumana ndi mavuto onenepa kwambiri<br />
kuposa ako.”<br />
Phunziro: Ukamakumana ndi mavuto, m’malo<br />
mongoganiza zodzipha, ndi bwino kumakumbukira kuti<br />
pali enanso amene akukumana ndi mavuto kuposa<br />
akowo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
39
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Akalulu ankafuna<br />
kudziponyera m’madzi?<br />
2. N’chiyani chinawapangitsa kusintha maganizo?<br />
3. Kodi ndi nyama ziti zimene mukuona kuti<br />
nazonso zimachita mantha kwambiri zikaona<br />
Achule?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
40
Ukakwera M’mwamba Usamatukwane<br />
Pansi<br />
Mnyamata wina anakwera padenga la nyumba ndipo<br />
atayang’ana pansi, anaona Nkhandwe ikudutsa pafupi<br />
ndi nyumbayo. Nthawi yomweyo anayamba<br />
kuinyogodola amvekere, “Ndiwe chigawenga komanso<br />
kapsala. N’chifukwa chiyani wabwera kuno kunyumba<br />
za anthu amtendere komanso abwino, kodi ulibe<br />
manyazi? N’chifukwa chiyani umakonda kupita<br />
m’malo amene anthu amadziwa kale makhalidwe ako<br />
ochititsa dambisi?” Itamva zimenezi, Nkhandweyo<br />
inayankha kuti, “Ukhoza kundinyoza mmene<br />
ungathere. Zimakhala zophweka kumadzitukumula<br />
komanso kumachita mwano utakwera padenga.<br />
Ndikulakalaka kuti tsiku lina uzidzabwebwetuka<br />
choncho uli pansipa.”<br />
Phunziro: Osamatha mawu zikakhala kuti zinthu<br />
zikukuyendera. Osamachita chipongwe ukakhala malo<br />
otetezeka, chifukwa nthawi ina udzachokapo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
41
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />
Mnyamatayu ankanyoza Nkhandwe ali padenga la<br />
nyumba?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti nthawi zina anthu<br />
amachitadi zangati zimenezi? Perekani chitsanzo.<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
42
Pansi pa Mtima<br />
Tsiku lina Gondwa anaba nkhuku pakhomo lina ndipo<br />
anakalowa nayo kuphanga lake. Atafika kuphangako<br />
anauza ana ake kuti waba nkhukuyo kukhomo<br />
lapafupi. Koma kuti aiwotche, ankafunika moto. Ndiye<br />
Gondwayo anaganiza zotuma mwana wake kuti<br />
akapale moto kukhomo anaba nkhuku lija. Anamuuza<br />
kuti, “Ndikufuna ukapale moto uko. Koma popeza<br />
nkhukuyi taba komweko, asakadziwe kuti tikufuna<br />
kudzawotchera nkhuku. Ndiye ngakhale<br />
akakukakamize, usakaulule kuti motowo<br />
tikudzachitira chiyani. Koma pansi pamtima<br />
uzingodziwa iweyo kuti tikufuna kudzawotchera<br />
nkhuku.” Kenako mwanayo ananyamuka n’kupita<br />
kukapala moto atatenga chiwaya chake. Atafika<br />
kumeneko, anagogoda ndipo ananena chimene<br />
wabwerera. Anthu amene anawapeza kunyumbako<br />
anayamba kumupanikiza ndi mafunso, amvekere,<br />
“Motowo mukufuna mukachite nawo chiyani?”<br />
Mwanayo anayankha kuti, “Anandiuzatu kuti<br />
ndisadzaulule. Amati ndizingodziwa ndekha, pansi<br />
pamtima wanga, kuti tikufuna kukawotchera<br />
nkhuku.” Anthuwo atangomva zimenezi anazindikira<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
43
kuti nkhuku yawo waba ndi Gondwa, ndipo<br />
anathamangitsa mwanayo mpaka kukafika paphanga<br />
lija. Kenako anatenga khasu n’kukumba phangalo<br />
ndipo anapha Gondwa ndi ana ake onse.<br />
Phunziro: Palibe chinsinsi padziko lapansi.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mwana wa Gondwa ananena chiyani<br />
atafunsidwa chifukwa chimene anapitira kukapala<br />
moto?<br />
2. Kodi zimene mwanayo ananena zinali zoona<br />
kapena zabodza?<br />
3. Kodi mwanayu analakwitsa kunena zinthu zina<br />
zimene bambo ake anamuuza kuti angozidziwa<br />
yekha? Ndiye tinganene kuti kunena zoona si<br />
kwabwino?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
44
Njoka Yopanda Pabwino<br />
Chaka china kunazizira kwambiri moti madzi ankatha<br />
kuuma gwa ngati mwala. Ndiye munthu wina, yemwe<br />
ankachokera kunkhalango, anaona njoka yakuda<br />
itagona m’mbali mwa nsewu. Njokayo inkaoneka kuti<br />
yangotsala pang’ono kutsirizika chifukwa cha kuzizira.<br />
Kenako munthuyo anaichitira chifundo ndipo anaitola<br />
n’kuiika mujuzi yake kuti imve kutentha. Atafika<br />
kwawo anaiika pafupi ndi moto kuti itenthedwe. Ana a<br />
munthuyo ankangoiyang’ana. Kenako Njokayo<br />
inayamba kumvako bwino, moti inayambiranso<br />
kuyenda bwinobwino. Ndiyeno mwana m’modzi<br />
anaganiza zoti aisisite, koma atangochita zimenezi,<br />
Njokayo inadzutsa mutu wake kuti imulume.<br />
Munthuyo atangoona zimenezo anatenga nkhwangwa<br />
yake n’kudula Njokayo pakati. Kenako anati, “Anthu<br />
ena alibe pabwino inu! Ukhoza kuwachitira chifundo<br />
koma sayamika, moti amalumanso dzanja limene<br />
likuwadyetsa. Munthu woti ndamupulumutsa,<br />
akufunanso kundiphera mwana!”<br />
Phunziro: Anthu oipa alibe pabwino.<br />
Mafunso<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
45
1. N’chifukwa chiyani munthu uja anatola Njoka?<br />
2. N’chifukwa chiyani Njokayo inkafuna kuluma<br />
mwana wa munthuyo?<br />
3. Kodi nkhaniyi ikusonyeza kuti munthuyo<br />
anaphunzirapo chiyani pa zimene zinachitikazo?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
46
Ntchentche Yosimbwa<br />
Kalelo kunali bambo wina wadazi. Bamboyo ankati<br />
akamaliza kudya nsima, ankakonda kukhala<br />
pakhonde kuti aphwetse mkhuto wake. Ndiye tsiku<br />
lina kunabwera Ntchentche n’kuyamba kumusokosa<br />
komanso kumuluma dazi lake. Kenako Ntchentcheyo<br />
inatera padazilo ndipo bamboyo anaganiza zoionetsa<br />
mbwadza poiphwanya ndi dzanja lake. Koma m’malo<br />
moti aphwanye ntchentcheyo, anamenya mutu wake,<br />
ndipo anamva ululu wosaneneka. Ntchentcheyo<br />
inapitirizabe kusimbwa, koma pa nthawiyi, nzeru<br />
zinamubwerera bamboyo moti sanalimbane nayo.<br />
Anati, “Umangodzivulaza wekha ukamalimbana ndi<br />
adani oipa.”<br />
Phunziro: Ukamalimbana ndi munthu woipa,<br />
umavutika ndi iweyo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
47
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani munthuyu anadzimenya<br />
m’mutu?<br />
2. N’chifukwa chiyani anaganiza zongosiya<br />
kulimbana ndi Ntchentcheyo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
48
Nkhandwe Ichezera Dokowe<br />
Kalekalelo Nkhandwe inali pa ubwenzi wa ponda apo<br />
m’pondepo ndi Dokowe. Ndiye tsiku lina Nkhandweyo<br />
inaitana Dokowe kuti akadye nkhomaliro kwawo.<br />
Koma Dokowe atafika, anapeza kuti wangomuphikira<br />
nsuzi ndipo anauika m’mbale yosalowa. Dokoweyo<br />
anayesetsa kuti amwe nsuziwo koma palibe chomwe<br />
anaphulapo. Nsuziwo unkangothera pamlomo wake<br />
wautali. Analimbana nawo kwa nthawi yaitali ndipo<br />
atatopa anangousiya, koma ali ndi njala kwambiri.<br />
Ndiye popeza paja amati, kwa eni kulibe mkuwo, mutu<br />
wa nkhuku n’chiwalo, dokowe sananene chilichonse.<br />
Anazindikira kuti mnzakeyo anachita izi pongofuna<br />
kumucheza basi. Kenako Nkhandwe inati, “Pepani kuti<br />
ndinakuphikirani nsuzi womwe simumaukonda.<br />
Ndikuona kuti udakali nde, mmene unalili.” Koma<br />
Dokowe anayankha kuti, “Usapepese ambwana,<br />
ndathokoza kwambiri chifukwa cha mtima wako<br />
wochereza alendo.” Kenako ananyamuka n’kuona<br />
msana wa njira. Ndiye tsiku lina, Dokowe nayenso<br />
anaitana mnzakeyu kuti akadye kwawo. Itangomva<br />
uthengawu, Nkhandweyo sinachedwechedwe, moti<br />
inauyamba ulendo wa kwa mnzakeyo. Itafika,<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
49
inamupeza akumudikirira ndipo inati, “Ndabwera<br />
bwanawe, paja okuluokulu odati kaitana kachita<br />
ujeni, ukachedwa ungakakapeze katabopha!”<br />
Mnzakeyo anaseka kwambiri ndipo kenako<br />
anamulowetsa m’nyumba kuti akadye zakudya<br />
zokoma zomwe anamukonzera. Zakudyazo anaziika<br />
mumtsuko wa kukamwa kwakung’ono, moti<br />
Nkhandwe sikadantha kulowetsa mutu wake n’kudya<br />
chakudyacho. Nkhandweyo inamva kuwawa mumtima<br />
mwake chifukwa cha zimenezi moti inangoyamba<br />
kunyambita kunja kwa mtsukowo. Ndiyeno Dokowe<br />
anati, “Sindipepesa ndi zimene zachitikazi, mwina<br />
ungaphunzirepo kathu. Nkhonya yobwezeratu<br />
imawawa?”<br />
Phunziro: Tizichitira ena zimene ifenso timafuna<br />
atatichitira.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
50
Mafunso<br />
1. Kodi Nkhandwe inachitira bwanji Dokowe<br />
chipongwe?<br />
2. Nanga Dokowe anachita chiyani atazindikira<br />
zimenezi?<br />
3. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani tinganene<br />
kuti Nkhandwe ndi Dokowe sanali mabwenzi a<br />
pamtimadi?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
51
Nkhandwe Itola Chigoba<br />
Tsiku lina Nkhandwe inalowa m’chipinda china<br />
chomwe anthu ochita zisudzo ankasungamo zinthu<br />
zawo. Mwadzidzidzi, Nkhandweyo inaona nkhope ya<br />
munthu ikumuyang’ana ndipo inayamba kuchita<br />
mantha. Koma itayang’anitsitsa bwinobwino inaona<br />
kuti chinali chigoba chomwe ochita zisudzo ankavala<br />
akamachita sewero. Ndiyeno Nkhandweyo inati, “Kani<br />
ndi iweyo? Umaonekatu ngati ndiwe munthu<br />
weniweni. Koma n’zomvetsa chisoni kuti ulibe<br />
ubongo.”<br />
Phunziro: Osamapusitsidwa ndi maonekedwe akunja.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkachita<br />
mantha itaona chigoba?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nkhandweyo inauza<br />
chigobacho kuti, “N’zomvetsa chisoni kuti ulibe<br />
ubongo”?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
52
Timba Atengeka Ndi Mbalame Zokongola<br />
Tsiku lina Timba anapita kukawongola miyendo<br />
kumalo amene mbalame zina zokongola kwambiri<br />
zotchedwa Pikoko zinkakonda kukhala, ndipo anatola<br />
nthenga zososoka za mbalamezo n’kuzimangirira<br />
kuchipsepse chake n’kumayenda moyerekedwa,<br />
kwinaku akulowera kumene kunali mbalamezo. Ndiye<br />
mbalamezo zitamuona, zinakwiya kwambiri moti<br />
zinamugwira n’kumuchotsa nthenga anamanga<br />
kuchipsepse zija. Chifukwa cha manyazi, Timbayo<br />
anabwerera kumene kunali mbalame zinzake, zomwe<br />
zinkaona zimene zinkachitikazo zili chapatali.<br />
Anzakewo anamukwiyira kwambiri ndipo anamuuza<br />
kuti, “Si kukongola kwa nthengatu kumene<br />
kumapangitsa mbalame kukhala yabwino, koma<br />
mtima.”<br />
Phunziro: Maonekedwe akunja sanena zambiri za<br />
mtima wa munthu.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
53
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani mbalame zokongola<br />
zinazula nthenga pa chipsepse cha Timba?<br />
2. N’chifukwa chiyani anzake a Timba<br />
anakhumudwa ndi zimene mnzawo anachitazi?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
54
Kudzitama Kunaphetsa Chule<br />
Tsiku lina Chule ndi bambo ake anakhala m’mbali<br />
mwa dziwe n’kumawothera dzuwa. Chuleyo anauza<br />
bambo ake kuti, “Bambo, dzulo ndinaona chinthu<br />
chachikulu koopsa. Chinalitu chachikulu, chachikulu<br />
zedi ngati phiri. Chinali ndi nyanga ziwiri zikuluzikulu<br />
pamutu pake, chimchira chachitali komanso<br />
dzimapazi zikuluzikulu.” Kenako bamboyo anati,<br />
“Takhala chete iwe, imene ukunenayotu ndi Ng’ombe<br />
ya mlimi wa pamtundapo. Koma sikuti ndi yaikulu<br />
mmene ikuneneramo, ukungokokomeza iwe!<br />
Yangokhala yaitaliko pang’ono poyerekeza ndi ineyo,<br />
moti nanenso nditadzifufumitsa ndikhoza kufanana<br />
nayo. Dikira uone . . . .” Kenako Chuleyo anakokera<br />
mpweya n’kudzifufumitsa kwambiri. Ndiyeno anafunsa<br />
mwana wakeyo kuti, “Kodi ng’ombeyo inali yaikulu<br />
chonchi?” Mwanayo anayankha kuti, “Ayi, inali<br />
yaikulu kuposa pamenepo.” Chuleyo anapitirizabe<br />
kukokera mpweya ndipo anadzifufumitsa,<br />
n’kudzifufumitsa kenako n’kudzifufumitsa. Ndiyeno<br />
anafunsa kuti, “Nanga bwanji pamenepo?” Mwanayo<br />
anayankhanso kuti, “Ayi, inali yaikulu, yaikulu<br />
kwambiri kuposa pamenepo.” Ndiyetu Chule<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
55
wamkuluyo anakoka mpweya, kuukoka, n’kuukoka<br />
moti anafufuma, kufufuma kenako n’kufufuma.<br />
Ndiyeno anati, “Ndikuganiza kuti Ng’ombeyo sinali<br />
yaikulu kuposa apa . . . ” Atangonena zimenezi, nthawi<br />
yomweyo anaphulika.<br />
Phunziro: Kufuna kuoneka wochenjera kumabweretsa<br />
mavuto.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani chule wamng’ono<br />
ankaganiza kuti waona chilombo chachikulu<br />
koopsa?<br />
2. Mukuganiza kuti n’chiyani chinachititsa kuti<br />
bambo a Chuleyo asonyeze mwana wakeyo kuti<br />
akhoza kufanana ndi chilombocho?<br />
3. N’chiyani chinapangitsa kuti bamboyo<br />
aphulike?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
56
Ubwenzi wa Mkango ndi Kapolo<br />
Tsiku lina kapolo wina anathawa kwawo n’kulowa<br />
m’nkhalango ina. Pamene ankayendayenda<br />
m’nkhalangomo anakumana ndi Mkango womwe<br />
unkabagula. Atangouona anatembenuka n’kuyamba<br />
kuthawa, koma anadabwa atazindikira kuti mkangowo<br />
sukumuthamangitsa. Kenako anaima n’kubwerera<br />
kumene kunali Mkango uja. Pamene ankauyandikira,<br />
mkangowo unamuonetsa dzanja lake lomwe<br />
linkatuluka magazi. Kapoloyo anaona minga yaikulu<br />
yomwe inabaya mwendo wa mkangowo ndipo<br />
unkamva ululu wosaneneka. Kapoloyo anamva chisoni<br />
kwambiri moti anachotsa mingayo n’kumangapo<br />
nsanza. Atangomaliza kuchita zimenezi, Mkangowo<br />
unadzuka n’kuyamba kunyambita kapoloyo ngati<br />
mmene amachitira galu. Kenako unatenga kapoloyo<br />
n’kupita naye kuphanga lake ndipo tsiku lililonse<br />
unkamubweretsera nyama yoti adye. Koma pasanapite<br />
nthawi, Mkangowo komanso kapoloyo anagwidwa ndi<br />
anthu a kumudzi anathawa kuja. Chifukwa choti<br />
kapoloyo anathawa mbuye wake anaweruzidwa kuti<br />
aphedwe pomusiya kuti adyedwe ndi mkango. Kenako<br />
anasiya Mkangowo osaupatsa chakudya kwa masiku<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
57
angapo kuti akadzangoumasura, udzapwepwete ndi<br />
mafupa omwe. Mfumu komanso anthu a m’mudzimo<br />
anasonkhana pabwalo lina kuti aone zimenezi<br />
zikuchitika ndipo asilikali anagwira kapolo uja<br />
n’kumapita naye kumene kunali Mkango kuja. Kenako<br />
asilikali anamasula chingwe chomwe anamangira<br />
Mkangowo ndipo unayamba kuthamanga ukubangula<br />
n’kumapita komwe kunali kapolo uja. Koma<br />
Mkangowo utayandikira, unazindikira kuti ndi bwenzi<br />
lake lomwe linamusamalira atavulala. Moti unagona<br />
pansi pafupi ndi kapoloyo n’kuyamba kunyambita<br />
manja ake monga mmene amachitira galu. Mfumu ya<br />
mudziwo inadabwa ndi zimenezi ndipo inaitanitsa<br />
kapoloyo. Kapoloyo anafotokoza zonse zomwe<br />
zinachitika ndipo Mfumuyo inakhululukira kapoloyo.<br />
Mkango ujanso unamasulidwa n’kupita kunkhalango.<br />
Phunziro: Ukamachitira ena zabwino, nawonso<br />
amadzakuthandiza zikadzakusokonekera.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
58
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani kapolo anathandiza<br />
Mkango?<br />
2. N’chiyani chinachititsa kuti Mkango ndi<br />
kapoloyo azigwirizana?<br />
3. Kodi mfumu inaphunzirapo chiyani pamene<br />
kapoloyo anafotokoza zimene zinachitika kuti<br />
Mkangowo usamudye?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
59
Mleme Uchenjera Pogona<br />
Pa nthawi ina, zilombo zakuthengo ndi mbalame<br />
zinayambana moti panakonzedwa zoti pachitike<br />
nkhondo. Ndiye mbalame zinayamba kusonkhanitsa<br />
asilikali ake, nazonso zilombo zinayamba kuchita<br />
chimodzimodzi. Koma Mleme unkakana kulowa ku<br />
gulu lililonse. Mbalame zinkati zikauuza kuti ukhale<br />
msilikali unkati: “Inetu ndili m’gulu la zilombo, siine<br />
mbalame.” Komanso zilombo zikauuza kuti, “Bwera<br />
udzalowe gulu lathu,” ankayankha kuti, “Inetu ndine<br />
mbalame, ndiye ndilowa bwanji m’gulu lanu?” Koma<br />
mwamwayi, nkhondo ija inalephereka ndipo mbalame<br />
komanso zilombo zakuthengo zinagwirizana<br />
zokhazikitsa mtendere. Kenako mbalame komanso<br />
zilombo zija zinakonza phwando lokondwerera kuti<br />
nkhondoyo yalephereka. Ndiye mleme unaganiza<br />
zokasangalala nawo ndipo unapita kumene kunali<br />
mbalame koma mbalame zonse zinagwanda. Kenako<br />
unauluka n’kupita kumene kunali zilombo<br />
zakuthengo. Koma nazonso zinamukana ndipo<br />
zinamuuza kuti akapanda kunyamuka zikuonetsa<br />
zakuda. Mlemewo unadandaula kwambiri ndi zimenezi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
60
ndipo unati, “Ukakhala kuti suli m’gulu lililonse,<br />
umakhala wekha.”<br />
Phunziro: Osamafuna anzathu pakakhala pamtendere.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Mleme unakana kukhala<br />
m’gulu la mbalame komanso la zinyama?<br />
2. N’chifukwa chiyani mbalame komanso zinyama<br />
zinakana Mleme atabwera kuti adzasangalale<br />
nawo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani pamenepa?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
61
Nkhani ya Mbawala ndi Mlenje<br />
Tsiku lina Mbawala inkamwa madzi ndipo inayamba<br />
kugomera chithunzithunzi chake chomwe<br />
chinkaoneka m’madzi. Kenako inati, “Ndi ndani<br />
winanso amene ali ndi nyanga zokongola chonchi<br />
m’nkhalango muno?” Kenako inayang’ana miyendo<br />
yake n’kunena kuti, “Ndimalakalaka ndikanakhala ndi<br />
miyendo yolongosoka yoti izigwirizana ndi nyanga<br />
zamtengo wapatali zomwe zili m’mutu mwangazi.<br />
Zimandiwawa kwambiri ndikaganizira kuti miyendo<br />
yanga ndi yoonda ngati zotokosera m’mano.” Mawu<br />
amenewa ali m’kamwa, kunatulukira mlenje ndipo<br />
anayamba kuithamangitsa. Koma chifukwa choti<br />
miyendo yake ndi yopepuka, Mbawalayo<br />
inangotsomphoka n’kuthawa, moti posapita nthawi<br />
inali patali kwambiri. Mbawalayo inapitirizabe<br />
kuthamanga ndipo inasiya kuyang’ana komwe<br />
imapita, moti inalowa m’ziyangoyango. Chifukwa cha<br />
kukula kwa nyanga zake, inakanirira<br />
m’ziyangoyangozo ndipo mlenje uja anaipeza<br />
n’kungoitola. Mbawalayo inayamba kulira ndipo<br />
mumtima mwake inkati, “N’chifukwa chiyani<br />
timakonda kunyoza zinthu zomwe zimatithandiza<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
62
kwambiri, n’kumakonda zinthu zomwe zikhoza kutiika<br />
m’mavuto?”<br />
Phunziro: Zinthu zimene zimaoneka zonyozeka<br />
m’zimene zimatithandiza kuti tikhale ndi moyo.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani mbawala inkafuna kukhala<br />
ndi miyendo yokongola?<br />
2. Kodi n’chiyani chinachititsa kuti Mbawala<br />
igwidwe?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
63
Njoka Ipsa Mtima<br />
Tsiku lina njoka inalowa m’nyumba ya munthu wina<br />
momwe munali zitsulo komanso zinthu zina.<br />
Ikuyenda, njokayo inayamba kukandidwa ndi chitsulo<br />
chinachake, moti inapsa mtima n’kuyamba<br />
kuchimenya. Itaona kuti palibe chimene chimachitika<br />
inangosiya kulimbana ndi chitsulocho n’kumapita.<br />
Inkaona kuti ikhoza kungotaya nthawi yake<br />
kumalimbana ndi chinthu chomwe sichimva<br />
kupweteka.<br />
Phunziro: N’kupanda nzeru kumalimbana ndi chinthu<br />
chomwe sichimva kupweteka.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi n’chifukwa chiyani njoka inayamba<br />
kumenya chitsulo?<br />
2. Kodi mungapereke chitsanzo cha zimene anthu<br />
amachita zomwe zimakhala ngati kulimbana ndi<br />
chitsulo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
64
Mitengo Inadzipweteketsa<br />
Tsiku lina munthu wina anapita kunkhalango<br />
nkhwangwa ili m’manja. Munthuyo ankapita<br />
kunkhalangoko kuti akapemphe nthambi ya mtengo<br />
woti aike kunkhwangwa yakeyo, ndipo anauza<br />
mitengo yomwe anaipeza m’nkhalangomo kuti<br />
imuchitire chifundo n’kumupatsa zomwe amafunazo.<br />
Mitengoyo itamva dandauloli, inafunsa munthuyo kuti<br />
akufuna akachite chiyani ndi nkhwangwayo akaika<br />
nthambiyo. Munthuyo anayankha kuti, “Ndikufuna<br />
ndikachitire zinthu zofunika kwambiri.” Popeza<br />
mitengo inali yachifundo, inapatsa munthuyo zomwe<br />
ankafuna. Kenako munthuyo anatenga mtengowo<br />
n’kuika kunkhwangwayo ndipo anayamba kugwetsa<br />
mitengo ya m’nkhalangomo. Mitengoyo itaona zimenezi<br />
inayamba kudandaula kuti sinaganize bwino popereka<br />
kwa mdani wawo chida choti awaphere.<br />
Phunziro: Osamapereka chida kwa mdani wako<br />
chifukwa akhoza kukuphera chomwecho.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
65
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti mitengo sinkadziwa<br />
chimene munthuyo ankafuna kuchita ndi<br />
nkhwangwa yomwe inali m’manja mwake?<br />
2. Kodi mitengo ikanapewa bwanji mavuto amene<br />
anabwera pambuyo pake?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
66
Galu Akumana ndi Nkhandwe<br />
Nkhandwe inali itatheratu chifukwa cha njala pamene<br />
inakumana ndi Galu wina yemwe ankangodziyendera.<br />
Galuyo anati: “Oo! kodi ndi abwenzi? Inetu<br />
ndinkadziwa kuti moyo wanu wosakhazikikawu<br />
udzakubweretserani mavuto. Mufa ndi njalatu! Bwanji<br />
osamagwira ntchito ngati mmene ndimachitira ine kuti<br />
muzipatsidwa chakudya nthawi zonse?” Nkhandweyo<br />
inati, “Apo ndiye sindingakutsutse m’bale wanga.<br />
Ngati mwayi utapezeka ndikhoza kuchita zomwezo.”<br />
Kenako Galuyo anati, “Tiye tipite kwa abwana anga<br />
ndipo uzikagwira ntchito imene ndimagwira. Ngati<br />
utamakagwira ntchito molimbikira, ukhoza<br />
kudzakhala Nkhandwe yodya bwino.” Kenako nyama<br />
ziwirizi zinauyamba ulendo wopita kunyumba kwa<br />
galu. Koma zili m’njira, Nkhandwe inaona kuti pakhosi<br />
pa Galu panali poperepeseka ndipo inafunsa kuti,<br />
“Kodi khosi lakoli linatani bwanawe?” Galuyo<br />
anayankha kuti, “Aaa, ndi mmene lilili. Pamenepa<br />
m’pamene pamadutsa kolala. Pakolala imeneyo ndi<br />
pamene amakolekapo chingwe chomwe amandimanga<br />
nacho ndikamagwira ntchito usiku. Nthawi zina<br />
chimapana pakhosipa ndithu, n’chifukwa chake<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
67
ubweya wina wasosokapo. Koma aa ndi zazing’ono,<br />
ukazolowera monga mmene ndinachitira ineyo.”<br />
Kenako nkhandweyo inati, “Umenewotu ndi moyo<br />
wovuta, kwathu timakhala mwaufulu ife. Basi tionana,<br />
ndikupita kwathu ine.”<br />
Phunziro: Ndibwino kumaonda uli paufulu kusiyana<br />
ndi kumanenepa uli kapolo.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Galu ankafuna kuthandiza<br />
Nkhandwe?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inaganiza<br />
zokana mwayi wa ntchito womwe Galu<br />
anamupezera?<br />
3. Kodi pali nthano iliyonse yomwe munaimvapo,<br />
yomwe ikugwirizana ndi nkhaniyi?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
68
Ziwalo Ziukira Mimba<br />
Tsiku lina ziwalo za thupi zinakwiya kwambiri.<br />
Ziwalozi zinkaona kuti zimagwira ntchito yotopetsa,<br />
pomwe mimba imangokhala, koma n’kumadya<br />
zakudya zonse. Choncho zinachita msonkhano ndipo<br />
zitakambirana, zinagwirizana kuti zinyanyale ntchito.<br />
Zinanena kuti ziyambiranso pokhapokha mimba<br />
ikavomera kuti izigwira nawo ntchito. Ndiyeno kwa<br />
masiku angapo, mikono inkakana kunyamula<br />
chakudya kupititsa pakamwa. Nalonso kamwa<br />
linkakana kulandira chakudya. Zimenezi zinachititsa<br />
kuti mano azisowa ntchito yoti agwire. Kenako ntchito<br />
zonse zinaimiratu. Koma patatha masiku atatu, ziwalo<br />
zija zinayamba kufooka. Manja ankalephera kusuntha<br />
komanso miyendo inkalephera kuima. Pamapeto pake<br />
ziwalozo zinaona kuti nayonso mimba inkagwira<br />
ntchito yotamandika zedi, ngakhale inali yosaonekera.<br />
Zinaonanso kuti chiwalo chilichonse chimagwira<br />
ntchito yaikulu kuti zinthu ziziyenda bwino.<br />
Phunziro: Mgwirizano umathandiza kuti zinthu<br />
ziyende.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
69
Mafunso<br />
1. Kodi ziwalo zina zija zinkafuna kuti mimba<br />
izichita chiyani?<br />
2. Kodi zinachita chiyani pofuna kukakamiza<br />
mimba kuti nayonso izigwira ntchito?<br />
3. Kodi ziwalo zinazo zinaphunzirapo chiyani?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
70
Mlimi Agwira Gwape Atabisala<br />
Tsiku lina Mlenje ankathamangitsa Gwape ndipo<br />
anam’tengetsa kwambiri moti anangotsala pang’ono<br />
kumugwira. Koma Gwapeyo anathawa n’kukalowa<br />
m’nkhola la mlimi wina n’kudzikwirira ndi zakudya za<br />
Ng’ombe. Miyendo yake yokha ndi imene inkaonekera.<br />
Kenako Mlenje uja anafika pakhomo pa Mlimiyo ndipo<br />
anafunsa mwana wa pakhomopo kuti, “Kodi unaona<br />
Gwape atadutsa apa?” Mwanayo ananena kuti<br />
sanamuone ndipo anayang’anayang’ana m’nkhola<br />
komanso malo ena a pafupi koma sanamupeze.<br />
Ataona kuti zamuvuta, Mlenjeyo anaona msana wa<br />
njira. Kenako Mlimi yemwe anali mwini malowo<br />
anatulukira ndipo atayang’ana m’khola la ng’ombelo<br />
anaona kuti simukuoneka mmene mumaonekera<br />
nthawi zonse. Anayamba kuloza kumene kunali<br />
zakudya za Ng’ombe kuja n’kunena kuti, “Kodi<br />
mitengo ikuoneka pali zakudya za Ng’ombepo ndi ya<br />
chiyani?” Kenako mwana wake uja anapita pamene<br />
panali zakudyazo ndipo atakoka mitengoyo<br />
anangozindikira kuti akukoka Gwape.<br />
Phunziro: Chule anadabwa m’madzi muli mwake.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
71
Mafunso<br />
1. Kodi n’chiyani chinachititsa kuti Mlimiyu<br />
agwire Gwape?<br />
2. Kodi n’chifukwa chiyani mnyamata uja<br />
komanso Mlenje uja analephera kuona Gwapeyo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
72
Nkhandwe M’munda wa Mpesa<br />
Tsiku lina Nkhandwe inkayenda m’munda wina ndipo<br />
inafika pamalo ena pomwe panali zipatso za mpesa<br />
zomwe zinkaoneka kuti ndi zakupsa, koma kungoti<br />
zinali zitayanga pamtengo wautali. Itaona mphesazo,<br />
Nkhandweyo inati, “Ndidye mpesazi kuti ndiphe<br />
ludzu.” Kenako inabwerera m’mbuyo n’kudumpha,<br />
koma sinafike pamene panali mpesazo. Inabwereranso<br />
m’mbuyo koma inaphonyanso. Inachita zimenezi<br />
kambirimbiri, koma palibe chomwe inaphulapo.<br />
Kenako inatopa ndipo inanyamuka n’kumapita kwawo<br />
itaimika mphuno zake m’mwamba, kwinaku ikunena<br />
kuti, “Ndikuganiza kuti mphesa zimenezi ndi zowawa.”<br />
Phunziro: Zimakhala zosavuta kumanyoza zinthu<br />
zomwe zakukanika kuzipeza.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inasiya mpesa?<br />
Kodi tinganene kuti simazifuna?<br />
2. N’chifukwa chiyani nkhandweyo inanena kuti<br />
mphesazo zinali zowawa?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
73
Ikakuthawa Imawawa Msuzi<br />
Munthu wina anagwira Njiwa ndipo anasangalala<br />
kwambiri chifukwa ankadziwa kuti nsima ya tsiku<br />
limenelo ikayenda. Koma ali mkati moganiza zimenezi,<br />
Njiwayo inamupulumuka n’kuthawa. Munthuyo<br />
anapsa mtima n’kuyamba kuikuwira Njiwayo<br />
n’kumaiuza kuti, “Iweeeeeeeee, umawawa msuzi!”<br />
Phunziro: Osamanyoza chinthu chikapita.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi munthuyu ankaganiza zochita nayo<br />
chiyani Njiwa anagwirayo?<br />
2. N’chifukwa chiyani Njiwayo itamupulumuka<br />
anaikuwira n’kuiuza kuti imawawa nsuzi?<br />
3. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />
anthu amanyoza chinthu chikapita? Chimakhaladi<br />
kuti ndi choipa? Fotokozani.<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
74
Hatchi Akhaulitsa Mphoyo<br />
Kalekalelo Hatchi ndi Mphoyo zinayambana, ndiye<br />
Hatchi anapita kwa Mlenje n’kumupempha kuti<br />
amuthandize kukhaulitsa Mphoyo. Mlenjeyo<br />
anavomeradi, koma anati: “Ngati ukufunadi kuti<br />
ndikuthandize kukhaulitsa mdani wakoyu, uyenera<br />
kumvera zimene nditakuuze. Undilole kuti<br />
ndizikutsogolera komanso ndimangirire chingwe ichi<br />
pakamwa pako kuti ndikakwera pamsana pakopa<br />
ndizichigwira kuti ndisagwe. Komanso ndiike chishalo<br />
ichi pamsana pako n’cholinga choti ndisamamve<br />
kupweteka ndikakhalapo.” Hatchiyo inagwirizana ndi<br />
zimenezi ndipo Mlenjeyo anachitadi zomwe<br />
anapanganazo. Zitatero, mothandizidwa ndi Mlenjeyo,<br />
Hatchiyo inakhaulitsadi Mphoyo ija. Kenako Hatchi<br />
inauza Mlenjeyo kuti, “Popeza zimene timafuna<br />
zatheka, tsikatu pamsana pangapa komanso chotsa<br />
chingwe wandimanga pakamwachi. Chotsanso<br />
chishalo chili pamsanachi.” Koma Mlenjeyo anati,<br />
“Osathamanga magazi a Hatchi, ndikusangalala<br />
kwambiri kukhala pamwamba pano, moti uiwale zoti<br />
nditsikapo.”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
75
Phunziro: Ngati utavomera kuti anthu akugwiritse<br />
ntchito pokwaniritsa cholinga chako, nawonso<br />
amakugwiritsa ntchito pokwaniritsa cholinga chawo.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Hatchi inapita kwa Mlenje?<br />
2. N’chifukwa chiyani Mlenje anathandiza Hatchi?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
76
Mbalame Yadyera<br />
Tsiku lina mbalame ina yotchedwa Pikoko inapita kwa<br />
Mulungu kukapempha kuti aipatse mawu anthetemya<br />
oti azigwirizana ndi kukongola kwake. Mulunguyo<br />
atamva pempho la mbalameyi anakana kuichitira<br />
zimene inkafunazo. Koma mbalameyi inakakamirabe<br />
ndipo inauza mulunguyo kuti amuchitire zimene<br />
amafunazo basi. Pofuna kukakamiza Mulunguyo kuti<br />
achite zimene inkafunazo, mbalameyi inauza<br />
Mulunguyo kuti amuchitire chifundo chifukwa<br />
m’mbuyomo mulunguyo anali atanenapo kuti<br />
mbalameyo ndi yokongola komanso yokondedwa<br />
kwambiri kuposa mbalame zonse. Koma Mulunguyo<br />
anaiuza mbalameyo kuti, “Uzikhutira ndi zimene uli<br />
nazo. Sungakwanitse kupeza chilichonse chimene<br />
ukufuna, komanso sungakhale katswiri pa<br />
chilichonse. Kusayamika bwanji, kukongolako<br />
sikumakukwanira?”<br />
Phunziro: Palibe munthu amene amadziwa zonse.<br />
Palibe munthu amene amakhala katswiri pa<br />
chilichonse.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
77
Mafunso<br />
1. Kodi mbalameyi inkafuna kuti Mulungu<br />
aichitire chiyani?<br />
2. N’chifukwa chiyani Mulungu anakana?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
78
Chizolowezi Chimabala Mwano<br />
Nkhandwe ina inamva zoti Mkango ndi woopsa<br />
kwambiri komanso kuti ndi Mfumu ya Nyama zonse.<br />
Ulendo woyamba umene Nkhandweyi inakumana<br />
nawo, inachita mantha kwambiri moti inaliyatsa liwiro<br />
n’kukabisala m’nkhalango. Koma itakumananso ndi<br />
Mkangowo ulendo wachiwiri, inaima patali<br />
n’kumauyang’ana ukudutsa. Koma kenako inatha<br />
mantha, ndipo itakumana nawonso ulendo wachitatu,<br />
inayamba kuyenda n’kumapita kumene kunali<br />
Mkangowo ndipo inaufunsa kuti mkazi ndi ana ake ali<br />
bwanji. Inafunsaso Mkangowo kuti, “Kodi<br />
tidzakumananso liti?” Kenako inatembenuka<br />
n’kumapita, kwinaku ikuyendetsa mchira wake<br />
mwamwano.<br />
Phunziro: Ukazolowerana ndi munthu umasiya<br />
kumulemekeza.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
79
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inachita mantha<br />
itakumana koyamba ndi Mkango?<br />
2. Kodi Nkhandwe inkachitanso mantha<br />
itakumana ndi Mkango ulendo wachitatu?<br />
N’chifukwa chiyani sinkachita mantha? Kodi<br />
Mkangowo unali utasintha?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
80
Munthu Atsutsana ndi Mkango<br />
Tsiku lina Munthu ndi Mkango ankakambirana kuti<br />
wamphamvu ndi ndani pakati pawo. Munthuyo<br />
ankanena kuti anthu ndi amphamvu kwambiri kuposa<br />
Mikango chifukwa ali ndi nzeru zambiri. Ndiyeno<br />
Munthuyo anauza Mkangowo kuti, “Tabwera kuno<br />
ndikuonetse chinthu chinachake kuti umvetse zoti<br />
anthu ali ndi mphamvu zoopsa.” Kenako anatengana<br />
ndi Mkangowo n’kupita nawo pamalo ena, ndipo<br />
anauonetsa chipilala cha Samisoni akukhadzula<br />
kamwa la Mkango ndi manja. Kenako Mkangowo<br />
unati, “Chabwino, koma zimene wandionetsazi si<br />
umboni woti anthu ndi amphamvu kuposa Mikango.<br />
Si, anthu ndi amene anapanga chipilalachi?”<br />
Phunziro: Munthu akhoza kukhotetsa nkhani kuti<br />
igwirizane ndi maganizo ake.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
81
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />
chipilala chinkasonyeza kuti Munthu ndi<br />
wamphamvu kuposa Mkango?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti Mkango ukanapanga<br />
chipilalacho, chikanakhala chosiyana ndi<br />
chimenechi? Nanga bwenzi chikuoneka bwanji?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
82
Nyerere Yanzeru<br />
Tsiku lina Chiwala chinkadumphadumpha, muluzi uli<br />
pakamwa ndipo chinkaoneka kuti sichikudandaula<br />
chilichonse. Kenako Nyerere inadutsa itanyamula<br />
thumba la chakudya ndipo inali ili thukuta<br />
kamukamu. Nyerereyi inkagwira ntchito yolemetsayi<br />
chifukwa inkafuna kuti isunge chakudya chambiri<br />
kuphanga lake kuti mvula ikadzayamba kugwa<br />
isadzavutike. Ndiye Chiwala chinafunsa nyerereyo<br />
kuti, “Bwanji osabwera kuti tidzacheze,<br />
ukudzizunziranji chotere ngati kapolo? Sunamvepo<br />
mwambi wakuti, papsa tonola sudziwa mtima<br />
wamoto? Ndani akudziwa ngati mawa tidzukenso?”<br />
Nyerereyo inayankha kuti, “Ndikusonkhanitsa<br />
chakudya choti ndidzadye mvula ikadzayamba.<br />
Nawensotu ungachite bwino kuchitiratu zimenezi<br />
nthawi ikadalipo.” Ndiyeno Chiwalacho chinayankha<br />
mwamwano kuti, “Ndivutikirenji kusunga chakudya<br />
choti ndidzadye mvula ikadzayamba, pomwe panopa<br />
chakudya chilipo kutapa kutaya!” Itamva zimenezi,<br />
Nyerereyo sidayankhe, inangopitirizabe kututira<br />
chakudya kuphanga lake. Pamene mvula inkayamba<br />
Chiwala chinalibe kalikonse ndipo pakhomo pake<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
83
panali galu wakuda. Chiwalacho chinkasirira chikaona<br />
Nyerere ikugawana chakudya ndi ana ake ndipo<br />
chinati, “Ukakhala ndi zambiri, ndi bwino kumasunga<br />
zina zoti udzagwiritse ntchito zikadzakuvuta.”<br />
Phunziro: Ukakhala ndi zochuluka kumasungako zina<br />
kuti udzagwiritse ntchito ukadzakumana ndi mavuto.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Nyerere inauza Chiwala<br />
kuti chisunge chakudya choti idzagwiritse ntchito<br />
m’nthawi yamvula?<br />
2. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
84
Mtengo ndi Bango<br />
Tsiku lina Mtengo unauza Bango lomwe linamera<br />
pafupi ndi phazi lake kuti, “Mwana iwe, n’chifukwa<br />
chiyani suzika kwambiri mizu yako n’kuimika mutu<br />
wako m’mwamba ngati mmene ndimachitira ine?”<br />
Bangolo linayankha kuti, “Ayi, ndimakhutira ndi<br />
mmene ndilili komanso zomwe ndimakwanitsa<br />
kuchita. Mwina ndimaoneka wofooka, koma ndimaona<br />
kuti ndimatetezeka mwa njira imeneyi.” Mtengo<br />
utamva zimenezi, nkhope yake inachita tsinya ndipo<br />
unati, “Umatetezeka? Iweyotu ndi woonda kwambiri<br />
moti umangokhala ngati uli ndi matenda a<br />
kaliondeonde, kathupi kako kamangoti<br />
lobodolobodooo. Mphepo ikamawomba umangoti<br />
tepatepa. Komansotu ndiwe wosavuta kuzula. Koma<br />
taona ifeyo, amunamuna ogona kukhomo kosatseka.<br />
Ndani angalimbe mtima kuti andizule ndi mitsitsi<br />
yomwe? Komanso ndi ndani amene angalimbe mtima<br />
kuweramitsa mutu wanga pansi?” Mawu amenewa ali<br />
m’kamwa, kunabwera chimphepo champhamvu ndipo<br />
mphepoyo inazula Mtengo uja ndi mitsitsi yomwe moti<br />
Mtengowo unangoti lambaaa, mutu utaloza pansi.<br />
Koma Bango lija linangopindikira kumene kumalowera<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
85
mphepo ndipo mphepoyo itadutsa, linadzukanso<br />
n’kukhala tsonga. Kenako linafunsa Mtengo uja kuti,<br />
“Waona, tsopano wamphamvu ndi ndani?”<br />
Phunziro: Osamadzitama.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Mtengo unauza Bango zinthu zotani?<br />
2. N’chifukwa chiyani Bango linkaona kuti ndi<br />
lotetezeka?<br />
3. Kodi mukuganiza kuti kudzitama<br />
kumabweretsa mavuto otani?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
86
Nkhandwe Yatulo<br />
Tsiku lina Nkhandwe inkacheza ndi Mphaka ndipo<br />
inayamba kudzitama n’kumanena kuti imadziwa<br />
kuzemba komanso kuthawa adani ake. Inati:<br />
“Sungakhulupirire, mwina ndingonena kuti ndili ndi<br />
kathumba kosatsegula ka njira zosiyanasiyana zomwe<br />
ndikhoza kugwiritsa ntchito pothawa adani anga.<br />
M’thumba limenelo muli njira zoposa 100 zomwe<br />
ndikhoza kusankha imene ndikufuna kugwiritsa<br />
ntchito.” Koma Mphaka anati, “Ineyo ndili ndi njira<br />
imodzi basi, komabe imandipulumutsa adani anga<br />
akamandithamangitsa.” Nthawi yomweyo panayamba<br />
kumveka phokoso la agalu ndipo linkamveka kuti<br />
likubwera kumene kunali Nkhandwe ndi Mphaka<br />
kuja. Mphaka atamva phokosolo, nthawi yomweyo<br />
anathawira mumtengo n’kukabisala, ndipo anauza<br />
Nkhandweyo kuti, “Ine ndimagwiritsa ntchito njira<br />
imeneyi. Nanga iweyo ugwiritsa ntchito njira iti?”<br />
Kenako Nkhandweyo inayamba kuganizira za njira<br />
yoyamba n’kuona kuti sikugwira. Inaganizira za njira<br />
ina n’kuonanso kuti sikugwira. Inapitirizabe<br />
kuganizira njira zina ndipo pa nthawiyi agalu aja anali<br />
akuyandikira. Kenako Nkhandweyo inasokonezeka<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
87
ndipo agaluwo anaigwira moti mwini agaluwo anaipha.<br />
Pamene zimenezi zinkachitika, mphaka uja<br />
ankangoonerera ndipo anati, “Bola kukhala ndi njira<br />
imodzi yothandiza, kusiyana ndi kukhala ndi njira<br />
zambirimbiri zomwe ukungoganiza kuti zikhoza<br />
kukuthandiza.”<br />
Phunziro: Ndi bwino kukhala ndi chinthu chimodzi<br />
chothandiza, kusiyana ndi kukhala ndi zambiri zomwe<br />
sizingakuthandize.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Nkhandwe inauza Mphaka chiyani?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inalephera<br />
kuthawa agalu?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
88
Mmbulu Inavala Chikopa cha Nkhosa<br />
Pa nthawi ina, Mmbulu unkakhaula ndi njala<br />
chifukwa zinali zovuta kuba Nkhosa. M’busa wa<br />
Nkhosazo anali watcheru kwambiri komanso anali ndi<br />
galu woopsa yemwe sankanyengerera akaona nyama<br />
ina ikuyandikira Nkhosa. Koma tsiku lina, Mmbuluwo<br />
unatola chikopa cha Nkhosa chomwe chinatayidwa,<br />
ndipo inavala chikopacho n’kulowa m’gulu la Nkhosa<br />
zija. Choncho mkazi wa Nkhosa yomwe inaphedwayo,<br />
anayamba kuchita chidwi ndi Mmbuluwo<br />
n’kumaganiza kuti ndi mwamuna wake. Ndiyeno<br />
Mmbuluwo unayamba kulowera kwina, kuchoka pa<br />
gulu la Nkhosalo ndipo Nkhosa yaikaziyo<br />
inkangotsatira. Kenako Mmbuluwo unagwira<br />
Nkhosayo n’kuidya. M’kupita kwa nthawi unazolowera<br />
kuba nkhosa mwa njira imeneyi, moti inadya nkhosa<br />
zambiri m’busa komanso galu uja osadziwa.<br />
Phunziro: Maonekedwe amapusitsa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
89
Mafunso<br />
1. Kodi Mmbulu unapusitsa bwanji Nkhosa?<br />
2. N’chiyani chinachititsa kuti Nkhosa yaikazi ija<br />
iganize kuti Mmbuluwo ndi mwamuna wake?<br />
3. Mungapereke zitsanzo cha zinthu zina zomwe<br />
zimaoneka ngati ndi zabwino koma zili zoopsa?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
90
Galu Apezeka Modyera Ng’ombe<br />
Tsiku lina Galu anatopa kwambiri ndipo ankafuna<br />
atabako tulo. Ndiye anakalowa m’khola la Ng’ombe<br />
n’kudziponya pamene panali zakudya za ng’ombezo.<br />
Pasanapite nthawi, Galuyo anayamba kuliza<br />
mkonono. Koma pa nthawiyi m’pamene Ng’ombe<br />
inatulukira ili ndi njala zedi ndipo sinachedwenso,<br />
koma kupita pamene panali zakudya zake. Ng’ombeyo<br />
inadzutsa Galu uja n’kumusokonezera maloto ake<br />
okoma. Galuyo anapsa mtima ndi zimenezi ndipo<br />
anayamba kuuwa, wuuuuuuuuu! Uwuuuuu!<br />
Ng’ombeyo imati ikati iyandikire zakudya zakezo,<br />
Galuyo ankauwa kwambiri ndipo ankafuna kuiluma.<br />
Kenako Ng’ombeyo inangomusiya ndipo inanyamuka<br />
n’kumapita kwinaku ikung’ung’udza kuti, “Aa, anthu<br />
ena amakonda kulusira anzawo pa zinthu zomwe<br />
sizingawathandize n’komwe.”<br />
Phunziro: Anthu ena amayambana ndi anzawo pofuna<br />
kuteteza zinthu zomwe sangazigwiritse ntchito<br />
komanso sizingawathandize.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
91
Mafunso<br />
1. Kodi Galu ankagwiritsa ntchito bwanji zakudya<br />
za Ng’ombe zija?<br />
2. N’chifukwa chiyani Ng’ombe inapita pamene<br />
Galu uja anagona?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
92
Fano Lathabwa<br />
Kalekalelo, anthu ena ankalambira miyala komanso<br />
mafano. Ankapempha milungu yawoyi kuti iwadalitse<br />
komanso iwathandize kupeza zimene akufuna pamoyo<br />
wawo. Koma panali munthu wina yemwe anali<br />
kwakwatuke wotheratu. Munthuyu ankapempha<br />
mulungu wake wathabwa kuti amuthandize, koma<br />
palibe chimene chinkachitika. Bambo ake ndi amene<br />
anamupatsa fanolo ngati cholowa. Munthuyu<br />
samatopa kupempha mulungu wakeyo kuti amupatse<br />
mwayi. Anachita zimenezi kambirimbiri, koma<br />
zinkangokhala ngati akulimbana ndi mtunda wopanda<br />
madzi. Tsiku lina, munthuyo anapsa mtima ndi<br />
mulungu wakeyo ndipo anamumenya mwamphamvu<br />
ndi chibakera ndipo mulunguyo anagwa pansi<br />
n’kusweka. Mkati mwa mulunguyo munatuluka<br />
ndalama zambirimbiri ndipo zinangoti mbweee<br />
m’nyumbamo. Munthuyo anangogwira pakamwa<br />
chifukwa chosowa chonena, ndipo anazindikira kuti<br />
bambo ake ndi amene anaika ndalamazo mkati mwa<br />
fanolo.<br />
Phunziro: Kulambira mafano kapena zinthu zina<br />
n’kosathandiza chifukwa zilibe moyo. Sizingakuuze<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
93
ngakhale zitakhala kuti munthu wina wabisa chuma<br />
mkati mwake. Lemba la Yesaya 44:14-17 limati: Pali<br />
munthu amene ntchito yake ndi yogwetsa mitengo ya<br />
mkungudza. Iye amasankha mtengo wamtundu<br />
winawake, waukulu kwambiri, n’kuusiya kuti ukule<br />
n’kukhwima pakati pa mitengo ya m’nkhalango. Iye<br />
anabzala mtengo wa paini, ndipo mvula yaukulitsa<br />
kwambiri. Tsopano mtengowo wafika poti munthu<br />
akhoza kuusandutsa nkhuni. Chotero iye watenga<br />
mbali ya mtengowo kuti asonkhere moto woti aziwotha.<br />
Wayatsa motowo n’kuphikapo mkate. Wasemanso<br />
mulungu woti azimugwadira. Mtengowo waupanga<br />
chifaniziro chosema ndipo akuchigwadira<br />
n’kumachilambira. Hafu ya mtengowo waitentha<br />
pamoto. Hafu ina ya mtengowo wawotchera nyama<br />
imene wadya, ndipo wakhuta. Wawothanso moto wake<br />
ndipo wanena kuti: “Eya! Ndafundidwa. Ndaona<br />
kuwala kwa moto.” Koma mtengo wotsalawo<br />
wapangira mulungu, wapangira chifaniziro chake<br />
chosema. Wachiweramira ndi kuchigwadira<br />
n’kumapemphera pamaso pake kuti: “Ndipulumutseni,<br />
pakuti ndinu mulungu wanga.” Munthu ameneyutu ndi<br />
wachaba. Chinthu wapanga yekhacho!<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
94
Mafunso<br />
1. Kodi munthuyo ankafuna kuti mulungu<br />
wakeyo amuchitire chiyani?<br />
2. N’chifukwa chiyani munthuyo anapsa mtima?<br />
3. Kodi tinganene kuti mulungu wakeyo<br />
anamuthandizadi?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
95
Msodzi<br />
Tsiku lina Msodzi anatenga chitoliro chake komanso<br />
ukonde wake n’kupita kumtsinje kuti akagwire<br />
nsomba. Atafika kumeneko, anapemphera kuti<br />
nsomba zibwere pamene anaika ukonde wakewo,<br />
koma palibe inabwera kapena kuonetsa mphuno yake<br />
pamwamba pa madzi. Kenako Msodziyo anakokera<br />
ukonde wakeyo chakumtunda ndipo<br />
anapempheranso. Mwadzidzidzi anangoona kuti mu<br />
ukondewo nsomba zayamba kuyenda pamwamba pa<br />
madzi komanso zina zikuphiriphitha, ndipo anati, “Aa,<br />
mwayamba kuvina ine ndikupemphera?” Ndiye<br />
nsomba yokalamba pa zonsezo inati, “Ukagwidwa ndi<br />
munthu wamphamvu, umafunika kumachita zimene<br />
akufuna.”<br />
Phunziro: Osamachita masewera ndi anthu<br />
amphamvu.<br />
Mafunso<br />
1. Msodziyo atagwira nsomba zija ndi ukonde<br />
wake, n’chifukwa chiyani nsomba zinayamba<br />
kuchita zimene msodziyo ankafuna? N’chifukwa<br />
chiyani mukutero?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
96
2. Kodi nsombazo zinkafunadi kuvina?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
97
Mnyamata Wabodza<br />
Kalekalelo kunali mnyamata wina yemwe ankaweta<br />
nkhosa yekhayekha pafupi ndi nkhalango ina<br />
yowirira. Mnyamatayu ankasowa wocheza naye ndipo<br />
ankangokhala yekhayekha tsiku lonse. Ndiye tsiku<br />
lina anapeza nzeru yomuthandiza kuti azisangalalako<br />
komanso kuti anthu azibwera n’kukhala naye pafupi.<br />
Anathamanga kumalowera kumene kunali mudzi<br />
wakwawo kwinaku akukuwa kuti, “Kuli Mikango, kuli<br />
Mikango kunoooooooooo!” Ndiye anthu a m’mudzimo<br />
anathamanga kudzakumana naye ndipo ena a iwo<br />
anaima limodzi naye kwa kanthawi<br />
n’kumamuyankhulitsa, moti panthawiyi<br />
sankasungulumwanso. Zimenezi zinamusangalatsa<br />
kwambiri, moti patapita masiku angapo, anachitanso<br />
chimodzimodzi. Ulendo umenewunso anthu a m’mudzi<br />
uja anabwera ndipo anakhala naye limodzi kwa<br />
nthawi yaitali ndipo mnyamatayo anasangalalanso<br />
kwabasi. Kenako anadzachitanso chimodzimodzi ndipo<br />
anthu a m’mudzi uja anatopa naye ndipo<br />
anam’tulukira kuti akungowapusitsa. Koma tsiku lina<br />
Mikango inatulukadi m’nkhalango ija ndipo inayamba<br />
kugwira Nkhosa zake. Mnyamatayo anayambanso<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
98
kukuwa kuti, “Kuli Mikango, kuli Mikango<br />
kunoooooooooo!” Anakuwa kwambiri kuposa<br />
poyamba, koma palibe anabwera. Anthuwo<br />
ankaganiza kuti mnyamatayo akungowanamiza ngati<br />
mmene anachitira maulendo ena aja. Mikangoyo<br />
inadya Nkhosa zambiri ndithu, ndipo itakhuta<br />
inabwerera m’nkhalango muja. Mnyamatayo<br />
anabwerera kumudzi kuja kwinaku akulira ndipo<br />
atafotokoza zimene zinachitika. Ndiyeno munthu wina<br />
wachikulire anamuuza kuti, “Anthu sakhulupirira<br />
munthu wabodza, ngakhale atakhala kuti akunena<br />
zoona.”<br />
Phunziro: Ukamanama anthu amakuzolowera, moti<br />
tsiku lina ukamadzanena zoona,<br />
samakukhulupiriranso.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
99
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani mnyamatayu ananena<br />
bodza?<br />
2. Kodi ndi mavuto ena ati amene akanabwera<br />
chifukwa cha bodza la mnyamatayu? Kodi<br />
tinganene kuti moyo wake unali pangozi?<br />
3. N’chifukwa chiyani anthu a m’mudzi uja<br />
sanakhulupirire ulendo womaliza womwe<br />
mnyamatayu ananena kuti kukubwera Mikango?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
100
Mpikisano wa Pakati pa Dzuwa ndi Mphepo<br />
Tsiku lina Mphepo komanso Dzuwa zinkatsutsana<br />
kuti wamphamvu ndi ndani pakati pawo. Mphepo<br />
inauza mnzakeyo kuti, “Inetu ndi wamphamvu zedi,<br />
ndimatha kuyalula denga la nyumba, kuzula mitengo<br />
komanso kugwetsa zinthu zikuluzikulu. Nditati<br />
ndifotokoze zonse zimene ndimachita, iweyo ukhoza<br />
kukalowa n’kutuluka, kenako n’kukalowanso.” Pa<br />
nthawiyi Dzuwa linkangomvetsera zimene mnzakeyo<br />
ankanena. Kenako anaona munthu akudutsa<br />
chapafupi, atavala chipewa. Ndiye Dzuwa linati,<br />
“Eyaaa, ndadziwa chochita tsopano. Kuti tidziwedi<br />
amene ali wamphamvu, tiye tipikisane. Tione amene<br />
angapangitse kuti munthuyo achotse chipewa<br />
chimene wavalacho.” Nthawi yomweyo Mphepo<br />
inasangalala ndipo inati, “Taulutsa zinthuzinthu ife,<br />
ndiye pali chiyani apaaa?” Kenako anagwirizana kuti<br />
iyambe Mphepo kuulutsa chipewacho. Koma Mphepo<br />
imati ikafuna kuulutsa chipewacho, munthuyo<br />
ankangochigwira n’kuchikhazikanso bwinobwino.<br />
Munthuyo ataona kuti Mphepo ikumuvutitsa,<br />
anangomanga chipewacho kuchibwano chake ndi<br />
chigwe. Mphepo inayesa kuulutsa chipewacho koma<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
101
inakanika ndipo inatopa kwambiri n’kukhala pansi<br />
kuti ipume. Kenako Dzuwa linalowa m’bwalo. Ndiye<br />
linaomba, n’kuomba ndipo kunja kunatentha zedi.<br />
Zitatero munthu uja anamva kutentha kwambiri ndipo<br />
anamasura chingwe chija n’kuvula chipewa chija.<br />
Kenako anakaima pamthunzi kuti mutu wake<br />
upitidwe mphepo.<br />
Phunziro: Osamadzitama, mwamuna mnzako ndi<br />
pachulu.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Mphepo inkaderera<br />
mphamvu za Dzuwa?<br />
2. Kodi tinganene kuti n’kulakwa kumadzitama?<br />
3. Kodi pamapeto pake ndi ndani amene<br />
anapambana?<br />
4. N’chifukwa chiyani Mphepo inalephera<br />
kuulutsa chipewa cha munthu uja?<br />
5. Kodi mukuganiza kuti Dzuwa likuimira<br />
chiyani?<br />
6. Nanga tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
102
Mnyamata wa Zala Zazitali<br />
Mnyamata wina anagwidwa ataba ndalama zambiri<br />
ndipo pofuna kuti ena atengerepo phunziro, mfumu ya<br />
m’deralo inalamula kuti aphedwe. Tsiku loti aphedwe<br />
litafika, mnyamatayo anapempha anthu omwe<br />
ankafuna kumupachikawo kuti amulole kuchita<br />
chinthu chimodzi asanaphedwe. Anapempha kuti<br />
akufuna auze mayi ake zinazake. Anthuwo<br />
anavomera, ndipo mnyamatayo anapita pafupi ndi<br />
mayi akewo n’kuwauza kuti, “Ndikufuna<br />
ndikunong’onezeni.” Mayiyo anaperekeradi khutu lake<br />
kuti mwana wakeyo amunong’oneze, koma mwanayo<br />
analuma khutulo ndipo linangotsala pang’ono<br />
kudukiratu. Anthu onse omwe anabwera<br />
kudzaonerera kuphedwa kwa mwanayo anadabwa ndi<br />
zimenezi ndipo ena ankati mchitidwe umenewu unali<br />
wankhanza zedi. Enanso ankanena kuti munthu<br />
wabwinobwino sangachite zomwe mnyamatayo<br />
anachita. Koma mnyamatayo anati: “Ndachita<br />
zimenezi kuti ndiwakhaulitse. Kungoyambira ndili<br />
mwana ndinkaba zinthu, koma ndikapita kunyumba,<br />
mayiwa ankalandira n’kusunga. M’malo moti<br />
andilangize kapena kundipatsa chilango, ankaseka<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
103
n’kunena kuti ‘palibe atadziwe zimenezi.’ Lero<br />
ndiphedwa chifukwa cha iwowa.” Atamva zimenezi,<br />
munthu wina wokonda kupemphera yemwe anali<br />
pamalopo anauza mayiyo kuti, “Mwanayu akunena<br />
zoona. Wafika pamenepa chifukwa inuyo<br />
munamulekerera. Pajatu amati, ‘Langiza mwana<br />
poyamba m’njira yake, ndipo ngakhale akadzakula<br />
sadzachokamo.’”<br />
Phunziro: Kumalangiza komanso kuphunzitsa ana<br />
adakali aang’ono.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mayiwa akanathandiza bwanji mwanayu<br />
ali wamng’ono?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti chinkapangitsa mayiyu<br />
kusapatsa mwana wakeyu chilango chinali<br />
chiyani?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
104
Bambo Yemwe Anakwatira Mitala<br />
Kalekalelo, amuna akuloledwa kukwatira akazi ambiri,<br />
bambo wina anakwatira akazi awiri. Wina anali<br />
wamkulu kwambiri kuposa msinkhu wake, ndipo<br />
winayo anali mtsikana. Akazi onsewa ankamukonda<br />
kwambiri ndipo aliyense ankafuna kuti mwamunayo<br />
azioneka mofanana naye. Wamkulu ankafuna kuti<br />
mwamunayo azioneka wachikulire, pomwe wamng’ono<br />
ankafuna azioneka wachinyamata. Ndiye n’kupita kwa<br />
nthawi, mwamuna uja anayamba kukalamba ndipo<br />
tsitsi lake linayamba kuyera. Mkazi wachitsikana uja<br />
anayamba kudana ndi tsitsi la imvilo chifukwa<br />
linkapangitsa kuti azioneka ngati anakwatiwa ndi<br />
mwamuna wamkulu kwambiri, ndipo ankaona kuti<br />
anthu azisokoneza n’kumaganiza kuti ndi bambo ake.<br />
Choncho tsiku lililonse mwamunayo akamagona,<br />
mkaziyo ankapesa tsitsi la mwamunayo n’kuthothola<br />
tsitsi lonse loyera. Koma mkazi wamkulu uja<br />
ankasangalala akaona kuti mwamuna wake wayamba<br />
kuchita imvi ndipo ankaona kuti zimenezi zithandiza<br />
anthu kuti asamaganize zoti mwamuna wakeyo ndi<br />
mwana wake. Choncho m’mawa ulionse mwamunayo<br />
asanadzuke, mkazi wamkuluyo ankathothola tsitsi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
105
lakuda lomwe linali m’mutu mwa mwamuna wakeyo.<br />
Pamapeto pake, tsitsi lonse la mwamunayo linatha<br />
ndipo anasanduka wadazi.<br />
Phunziro: Ukamangomvera aliyense, umasanduka<br />
chitsiru.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani mkazi wamkulu<br />
ankasangalala mwamuna wake atayamba imvi?<br />
2. Nanga n’chifukwa chiyani mkazi wamng’ono<br />
ankadana nazo?<br />
3. Kodi bamboyu anakumana ndi mavuto otani?<br />
4. Kodi n’zotheka kukhala wokalamba komanso<br />
wachinyamata nthawi imodzi?<br />
5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
106
Mayi ndi Nkhandwe<br />
“Ndati utontholeee!” Mawu amenewa anayankhula ndi<br />
Mayi wina ataima pazenera lotsegula. M’manja mwake<br />
munali mwana yemwe ankalira mosatonthozeka.<br />
Kenako mwanayo anatonthola ndipo Mayiyo<br />
anachenjeza mwanayo kuti, “Ukayambiranso kulira,<br />
ndikuponyera pazenerapa kuti Nkhandwe ikudye.”<br />
Ndiye zinangochitika kuti pa nthawi imene ankanena<br />
zimenezi, Nkhandwe inali ikudutsa chapafupi ndipo<br />
inamva zomwe mayiyo ananena. Nkhandweyo inaima<br />
pafupi ndi nyumbayo ndipo inayamba kudikira kuti<br />
mwanayo alirenso. Inati, “Lerotu ndiye ndachita<br />
mwayi. Ndikuganiza kuti alira posachedwapa, ana<br />
amakoma kwabasi moti nditsukako m’kamwa lero.”<br />
Nkhandweyo inadikira kwa nthawi yaitali, koma<br />
mwanayo sanalire. Kenako mwana uja anayambiranso<br />
kulira ndipo Nkhandweyo inaima pafupi ndi zenera lija<br />
kwinaku ikugwedezera mchira n’kumadikira kuti<br />
mayiyo aponye mwanayo pawindopo. Koma mayiyo<br />
anangotseka zeneraro n’kuyamba kumuyamwitsa.<br />
Posakhalitsa agalu a pakhomopo anatulukira n’kupeza<br />
Nkhandweyo ili pafupi ndi zeneraro ndipo<br />
Nkhandweyo inayamba kuthawa kwinaku ikunena<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
107
kuti, “Anthu ndi osathandiza, n’chifukwa chiyani<br />
nthawi zonse amapereka malonjezo akudziwa kuti<br />
sawakwaniritsa?”<br />
Phunziro: Anthu ambiri amalonjeza akudziwa kuti<br />
sakwaniritsa malonjezowo.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Mayiyu ankafunadi kutaya mwanayo<br />
pazenera?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inakhulupirira<br />
zimene Mayiyo ananena?<br />
3. N’chifukwa chiyani tinganene kuti sikuti panali<br />
ubwenzi uliwonse pakati pa Mayiyo ndi<br />
Nkhandwe?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
108
Msamuko wa Kamba<br />
Tsiku lina Kamba, kapena kuti Fulu, anapeza malo<br />
atsopano ndipo ankafuna kusamukira kumalowo.<br />
Ndiye anapempha mbalame ina yotchedwa Nkhwazi<br />
kuti imunyamule n’kukamusiya kumalowo ndipo<br />
analonjeza kuti aifumbatitsa kenakake. Nkhwaziyo<br />
inavomera ndipo inanyamula Kambayo itagwira<br />
chigoba chake n’kuuluka. Ili m’mwambamo,<br />
Nkhwaziyo inakumana ndi Mphamba. Mphambayo<br />
inauza Nkhwaziyo kuti, “Kambatu ndi ndiwo yokoma<br />
kwambiri.” Koma Nkhwaziyo inati, “Ukunena zoona,<br />
komatu chigoba chakechi n’cholimba ngati mwala.”<br />
Ndiyeno Mphambayo inati, “Utangomuponyera<br />
pamwala uwo, chigobacho chikhoza kusweka, ndipo<br />
ife tikhoza kukhwasula vankati.” Nkhwaziyo inamvera<br />
zimenezi ndipo inasiya Kambayo kuti akagwere<br />
pamwalawo moti chigoba chake chinaphwanyika.<br />
Nkhwazi komanso Mphambayo zinasangalala<br />
kwambiri ndi nyama yokoma yomwe zinadya patsikuli,<br />
moti zinachotsa dalazi.<br />
Phunziro: Osapereka moyo wako m’manja mwa mdani.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
109
Mafunso<br />
1. N’chiyani chimene Kamba analakwitsa?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti akanachita chiyani kuti<br />
akafike kunyumba yake yatsopano?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
110
Nkhanu ndi Mwana Wake<br />
Tsiku lina kunacha bwino kwambiri ndipo Nkhanu<br />
inatuluka m’nyumba limodzi ndi mwana wake<br />
n’kupita kukawongola miyendo m’mbali mwa mtsinje.<br />
Koma Nkhanuyo itaona mmene mwana wakeyo<br />
amayendera inati, “Mwana wanga, mayendedwe akowa<br />
sandisangalatsa. N’chifukwa chiyani ukuyenda<br />
cham’mbali? Mpofunika kuti uphunzire kumayenda<br />
mopita kutsogolo. Inetu ndikufuna uziyenda<br />
bwinobwino ngati munthu woti kutsogolo ukukuona.<br />
Sindikufuna uzindichititsa manyazi ndi mayendedwe<br />
ako osalongosokawo.” Koma mwanayo anayankha<br />
kuti, “Chabwino amayi, koma muyambe ndi inuyo<br />
kuchita zimenezi, kuti ineyo ndizitengera chitsanzo<br />
chanu. Anthutu amadabwa akamva munthu akunena<br />
kuti akufuna kusintha dziko, iyeyo akulephera<br />
kudzisintha yekha!”<br />
Phunziro: Osamauza ena kuti achite zomwe iweyo<br />
suchita.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
111
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti Nkhanu yaikuluyo<br />
inkayenda mopita kutsogolo?<br />
2. N’chifukwa chiyani mwanayo sanagwirizane<br />
ndi zimene kholo lake linanena?<br />
3. Kodi n’zotheka kuthandiza munthu wina<br />
kusintha, ifeyo tikulephera kudzisintha tokha?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
112
Bulu Avala Chikopa cha Mkango<br />
Bulu wina anatola chikopa cha Mkango chomwe alenje<br />
anachiyanika padzuwa kuti chiume. Buluyo anavala<br />
chikopacho ndipo anayamba kuyendayenda m’mudzi<br />
wonse. Anthu komanso nyama zimati zikangomuona,<br />
zinkalikumba liwiro, kufuna kupulumutsa moyo.<br />
Buluyo ataona fumbi limene linabwera chifukwa cha<br />
liwiro la anthu komanso nyama, anasangalala<br />
kwambiri ndipo anayamba kukuwa. Nthawi yomweyo<br />
anthu komanso nyama zinamuzindikira ndipo mwini<br />
Buluyo anabwera n’kuyamba kumukutumula. Kenako<br />
kunabwera Galu n’kuuza Buluyo kuti, “Ayi ndithu,<br />
mtima suvala nsanza. Nthawi zina ngakhale nkhuku<br />
ikhoza kumalota itavala nsapato! Komabe unaitha<br />
bwanawe, chifukwa unapusitsa ambiri. Koma<br />
ukudziwa kuti anakutulukira utangotsegula<br />
pakamwa?”<br />
Phunziro: Zovala zimapusitsa, koma zonena za munthu<br />
m’pamene umadziwa ngati ali wanzeru kapena ayi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
113
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Buluyo anasangalala<br />
pamene anthu komanso nyama zinkathawa?<br />
2. N’chiyani chinachititsa kuti anthu<br />
amuzindikire?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
114
Nkhani ya Mabwenzi a Pamtima<br />
Anthu ena awiri, omwe anali mabwenzi a ponda apo<br />
m’pondepo, anapita kukawongola miyendo<br />
kunkhalango ina, ndipo mwadzidzidzi anakumana ndi<br />
chimbalangondo. Chimbalangondocho chinayamba<br />
kupita kumene kunali anthuwo ndipo anachita<br />
mantha kwambiri. Munthu m’modzi anali kutsogolo<br />
ndipo wina anali m’mbuyo. Munthu anali kutsogoloyo<br />
atangoona kuti chilombocho chikubwera, analumphira<br />
mumtengo n’kubisala ndipo anasiya mnzakeyo ali<br />
pansi pomwepo. Winayo sanalimbanenso n’kuthawa,<br />
koma anangodziponya pansi ndipo nkhope yake<br />
inalowa m’dothi. Chimbalangondocho chinafika pafupi<br />
ndi munthu anagwera pansiyo ndipo chinatsitsa<br />
mphuno yake n’kuyamba kununkhiza mutu wa<br />
munthuyo. Mwamwayi chilombocho sichinamuchite<br />
kalikonse chifukwa chinkaganiza kuti wafa kale, paja<br />
zimbalangondo sizidya kapena kugwira chinthu<br />
chomwe chafa kale. Kenako chinanyamuka<br />
n’kumapita. Chitazimiririka, munthu anali mumtengo<br />
uja anatsika ndipo anafunsa mnzakeyo kuti, “Kodi<br />
bwanawe, chimbalangondo chija chimakunong’oneza<br />
chiyani?” Mnzakeyo anati, “Chinandiuza kuti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
115
ndisamakhulupirire mnzanga amene amandithawa<br />
zikavuta!”<br />
Phunziro: Osamakhulupirira munthu amene<br />
amakukonda zinthu zikakhala zikuyenda bwino, koma<br />
zikavuta amakuthawa.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Chimbalangondocho chinanong’onezadi<br />
munthu anali pansi uja?<br />
2. Kodi munthu anali mumtengo uja akanachita<br />
chiyani akanakhala kuti amamukondadi<br />
mnzakeyo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
116
Mapoto Awiri<br />
Tsiku lina mapoto awiri anasiyidwa m’mbali mwa<br />
mtsinje. Poto m’modzi anali wachitsulo ndipo wina<br />
anali wadothi. Ndiyeno mtsinjewo unadzadza madzi<br />
ndipo mapotowo anayamba kuyandama n’kumapita<br />
ndi madzi. Koma poto wadothiyo ankachita mantha<br />
ndipo ankayesetsa kusambira kuti asagundane ndi<br />
mnzakeyo. Poto wachitsuloyo anayamba kudabwa ndi<br />
zimenezi ndipo anakuwira mnzakeyo n’kumuuza kuti,<br />
“Usaope bwanaweee, sikuti ndikugundayi!” Koma poto<br />
wadothiyo anati, “Ndikuopa kuti ndikhoza kugundana<br />
nawe. Inetu ndinapangidwa ndi dothi, moti utati<br />
undigunde kapena ineyo nditati ndikugunde,<br />
ndingavutikebe ndi ineyo.”<br />
Phunziro: Anthu amphamvu ndi ofooka sangayendere<br />
limodzi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
117
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani tinganene kuti poto wadothi<br />
akanaphwanyika mosavuta akanagundana ndi<br />
mnzakeyo?<br />
2. Perekani zitsanzo za zinthu zamphamvu ndi<br />
zofooka zomwe sizingakhalire pamodzi?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
118
Ng’ombe Zinayi ndi Mkango<br />
Mkango wina unkazembekerera Ng’ombe zinayi zomwe<br />
zinkadya malo ena. Mkangowo unayesa maulendo<br />
angapo kuti ugwire Ng’ombezo koma unalephera.<br />
Unkati ukafuna kuti uukire Ng’ombe imodzi,<br />
Ng’ombezo zinkalozetsana mbuyo ndipo zinkapezeka<br />
kuti Mkangowo wakumana ndi nyanga za Ng’ombezo.<br />
Zikatere Mkangowo unkachita mantha n’kubwerera.<br />
Koma kenako Ng’ombezo zinayambana ndipo iliyonse<br />
inalowera kwake. Zimenezi zinachititsa kuti Mkango<br />
uja upezerepo mwayi, moti unayamba kugwira<br />
Ng’ombe imodziimodzi mpaka zonse zinatha psiti.<br />
Phunziro: Umodzi ndi mphamvu.<br />
Mafunso<br />
1. N’chiyani chinachititsa kuti Mkango usagwire<br />
Ng’ombe pamene zinkachitira zinthu limodzi?<br />
2. Kodi Ng’ombezo zikanatani kuti zisaphedwe ndi<br />
Mkango?<br />
3. Kodi anthu akagawikana, amakhala<br />
amphamvu kapena ayi?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
119
Mneneri Wabodza<br />
Kalekalelo kunali mneneri wina yemwe ankalosera<br />
zam’tsogolo. Ndiye m’nyengo ina ya mvula, mneneriyu<br />
anaona nyenyezi yachilendo ndipo anayamba kuuza<br />
anthu kuti, “Zaka 100 zikubwera kutsogoloku<br />
kudzachitika tsoka loopsa, anthu ambiri adzamwalira<br />
ndipo mudzi wonsewu udzatheratu.” Mneneriyo<br />
ankanena zimenezi akuyang’ana nyenyeziyo ndipo<br />
anaiwaliratu zoyang’ana pamene ankaponda. Ndiye<br />
mwatsoka, pansi panali mwala moti anapunthwa<br />
n’kugwa, nkhope yake n’kulowa m’matope. Anthu<br />
ataona zimenezi anayamba kumuseka ndipo<br />
anamufunsa kuti, “Kodi inuyo mumakwanitsa bwanji<br />
kumalosera zinthu zomwe zidzachitike zaka 100<br />
kutsogoloku, n’kumalephera kudziwa zimene<br />
zangotsala pang’ono kuchitikira phazi lanu? Ndiye<br />
mukufuna tizikhulupirira bodza bodza lofuka utsi<br />
limene mukutiuzali?”<br />
Phunziro: Kumayamba kaye wachotsa chitsotso cha<br />
m’diso lako kenako cha mnzako.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
120
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani anthu aja anayamba<br />
kuseka mneneriyu?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti ankakhulupirira kuti<br />
zimene ananenazo zidzachitikadi? Perekani<br />
chifukwa.<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
121
Msodzi Agwira Nsomba Yaing’ono<br />
Tsiku lina msodzi wina anapita kogwira nsomba koma<br />
sanagwire kathu tsiku lonse. Koma chakumadzulo<br />
anagwira kansomba kakang’ono. Kansombako<br />
kanayamba kupempha msodziyo kuti,<br />
“Ndikhululukireni bwana, ndisiyeni ndizipita. Ineyo<br />
ndidakali mwana, ndachepa kwambiri kuti ndidyedwe.<br />
Mukandibwezeretsa m’madzimu ndikula, ndipo<br />
mukhoza kudzandigwira nditanenepa m’tsogolo. Pa<br />
nthawiyo mukhoza kudzandidya ndili wonona<br />
kwambiri.” Koma msodziyo anati, “Ayi, ayi, sindilola.<br />
Ndagwira iweyo lero. Ndani akudziwa ngati<br />
ndingadzakugwiredi m’tsogolomo?”<br />
Phunziro: Osamawerengera zinthu zomwe sunapeze.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti nsomba yaing’onoyo<br />
ikanalola kuti idzagwidwenso ndi msodziyu ulendo<br />
wina?<br />
2. N’chifukwa chiyani nsombayo inauza msodziyo<br />
kuti amusiye? Kodi inkanena zoona?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
122
Munthu Wadyera Komanso Wansanje<br />
Anthu awiri omwe ankakhala moyandikana nyumba<br />
anapita kwa Mulungu ndipo anapempha Mulunguyo<br />
kuti awapatse zimene akufuna. Mmodzi wa anthuwo<br />
anali wadyera, pomwe winayo anali wansanje. Pofuna<br />
kuwakhaulitsa anthuwa, Mulunguyo anawauza kuti<br />
awapatsa zimene akufuna. Anawauzanso kuti<br />
aziwapatsa zimene akufuna koma anati azipereka<br />
kuwirikiza kawiri zimene m’modzi wapempha. Ndiyeno<br />
munthu wadyera uja anapempha kuti amupatse golide<br />
wodzaza nyumba yake. Pasanapite nthawi anapezadi<br />
golideyo ndipo anasangalala kwambiri. Koma<br />
chisangalalochi sichinakhalitse atazindikira kuti<br />
mnzake wansanje uja wapeza golide wodzadza nyumba<br />
ziwiri. Munthu wansanje uja anamvako bwino<br />
atazindikira kuti mnzake sakusangalala. Koma<br />
ankafuna kuti mnzakeyo akhaule kwambiri, moti<br />
anapempha Mulungu kuti amuchotse mnzakeyo diso<br />
limodzi. Zitatero, Mulungu anamuchotsadi mnzakeyo<br />
diso limodzi, koma zimenezi zinachititsa kuti iyeyo<br />
achotsedwe maso ake onse awiri, moti anakhala<br />
wosaona.<br />
Phunziro: Makhalidwe oipa amabweretsa mavuto.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
123
Mafunso<br />
1. Kodi ndi ndani amene anapezadi zimene<br />
ankafuna?<br />
2. N’chifukwa chiyani anthuwa sankakhutitsidwa<br />
ndi golide amene anali naye?<br />
3. Kodi mungatchule makhalidwe ena oipa amene<br />
amabweretsa mavuto?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
124
Khwangwala Waludzu<br />
Tsiku lina Khwangwala ankafuna kufa ndi ludzu.<br />
Koma mwamwayi anapeza mtsuko wamadzi. Koma<br />
atafika pafupi ndi mtsukowo anapeza kuti madzi ake<br />
anali ochepa ndipo anali pansi penipeni pa mtsukowo<br />
moti sankakwanitsa kuwamwa. Khwangwalayo<br />
anayesetsa kuti amwe madziwo koma analephera moti<br />
kenako anangowasiya n’kutsamira mtsukowo. Koma<br />
kenako nzeru zinamubwerera moti anatola mwala<br />
n’kuponyera mumtsukomo. Anatolanso mwala wina<br />
n’kuponya mumtsukomo ndipo madzi aja anayamba<br />
kukwera. Anapitirizabe kuchita zimenezi mpaka<br />
madziwo anakwera kwambiri ndipo anamwa n’kupha<br />
ludzu lake.<br />
Phunziro: Nyumba imayamba kumangidwa ndi njerwa<br />
imodzi.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi chikanachitika n’chiyani zikanakhala kuti<br />
Khwangwalayo anangokhala osachita chilichonse?<br />
2. Kodi n’chifukwa chiyani nthawi zina sibwino<br />
kutaya mtima mwansanga?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
125
Munthu Wam’nkhalango<br />
M’nyengo ina yozizira kwambiri munthu wina<br />
ankayenda usiku m’nkhalango ndipo anasokonekera<br />
n’kumalephera kupeza njira yakwawo. Ndiye pamene<br />
ankayendayenda m’nkhalangomo anakumana ndi<br />
munthu wina yemwe ankaoneka kuti ankakhala<br />
m’nkhalango momwemo. Munthuyo analonjeza kuti<br />
amupatsa malo ogona usikuwo komanso kuti kukacha<br />
amuthandiza kupeza njira yakwawo. Kenako<br />
munthuyo anamutenga n’kumapita naye kwawo koma<br />
munthu anasokonekera uja anaika manja ake<br />
pakamwa n’kumapemerera ndi mpweya wam’kamwa<br />
mwake. Ndiyeno munthu wam’nkhalango uja<br />
anafunsa kuti, “N’chifukwa chiyani mukupanga<br />
zimenezo?” Munthuyo anayankha kuti, “Manja anga<br />
azizidwa ndiye ndikufuna ndiwatenthetse ndi mpweya<br />
wochoka m’kamwa mwanga.” Kenako anafika<br />
kunyumba kwa munthu wam’nkhalango uja ndipo<br />
pasanapite nthawi anabweretsa phala lotentha<br />
kwambiri kuti mnzake uja adye. Ndiye munthu uja<br />
anayamba kudya phalalo ndipo asanaliike m’kamwa,<br />
ankalipemerera kaye. Ataona zimenezi, munthu<br />
wam’nkhalango uja anafunsa kuti, “Nanga mukuchita<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
126
zimenezo chifukwa chiyani?” Munthuyo anayankha<br />
kuti, “Phalali ndi lotentha kwambiri ndiye ndikuopa<br />
kuti lindiwaula m’kamwa. Choncho<br />
ndikumalipemerera ndi mpweya wam’kamwa mwanga<br />
kuti lizizire.” Atangomva zimenezi, munthu<br />
wam’nkhalango uja anati, “Basi tulukani m’nyumba<br />
mwanga muno! Munthu wamtundu wanji wotuluka<br />
mpweya wotentha komanso wozizira m’kamwa<br />
mwake.”<br />
Phunziro: Mupeze nokha.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mpweya wa munthuyu unali wotentha<br />
kapena wozizira?<br />
2. Kodi kuchita zinthu zimene tinazolowera<br />
n’kulakwa?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
127
Mazira Agolide<br />
Tsiku lina munthu anapita pachisa cha tsekwe ndipo<br />
anapeza dzira looneka lachikasu komanso lowala.<br />
Atalitola anaona kuti dziralo linkalemera kwambiri<br />
moti anaganiza zolitaya poganiza kuti munthu wina<br />
anaikapo mwala kuti amupusitse. Koma kenako<br />
anasintha maganizo ndipo anapita nalo kunyumba<br />
kwake. Atafika kunyumbako anazindikira kuti dziralo<br />
linali lagolide. Kenako anayamba kumapita kuchisa<br />
cha tsekwe chija m’mawa ulionse, ndipo ankatola<br />
dzira limodzi lagolide. Ankati akatola dzira limodzi,<br />
ankaligulitsa moti n’kupita kwa nthawi anakhala<br />
mponda makwacha. Munthuyo atayamba kulemera,<br />
anayamba dyera moti anaganiza zopeza mazira onse a<br />
tsekweyo nthawi imodzi. Choncho, anapha tsekwe uja<br />
n’kumung’amba pamimba ndipo mkati mwake<br />
sanapezemo kanthu.<br />
Phunziro: Dyera limatayitsa zambiri.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
128
Mafunso<br />
1. Kodi munthu wadyerayu ankaganiza kuti<br />
apeza chiyani mkati mwa tsekwe uja?<br />
2. Kodi anapezadi mazira agolide ambiri atapha<br />
tsekweyo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
129
Mbalame Yoimba Mokoma<br />
Kafansiyanji wina ankasowa tulo usiku ndipo<br />
ankangomvetsera mbalame ina ikuimba usiku wonse.<br />
Kaimbidwe ka mbalameyo kanamudolola kwambiri<br />
moti usiku wotsatira anagwira mbalameyo kuti<br />
izimuimbira nthawi zonse. Kenako anaiuza mbalameyo<br />
kuti, “Ndiye popeza ndakugwira, uzindiimbira nyimbo<br />
nthawi iliyonse imene ndikufuna.” Koma mbalameyo<br />
inati, “Mbalame za mtundu wathuwutu sizitha kuimba<br />
nyimbo ngati zikukakamizidwa komanso ngati<br />
zitatsekeredwa m’kanyumba.” Ndiye kenako munthu<br />
uja anati, “Ndiye ndikudyatu! Ndinamva zoti mbalame<br />
ngati iweyo mumakoma kwambiri mukakazingidwa<br />
m’mafuta.” Mbalameyo itangomva zimenezi inati, “Ayi,<br />
musandiphe. Ingondisiyani ndipo ndikuuzani zinthu<br />
zitatu zomwe zingakuthandizeni kwambiri kuposa<br />
kudya kathupi kanga kakang’onoka.” Ndiyeno munthu<br />
uja anaimasula n’kuisiya ndipo mbalameyo inaulukira<br />
panthambi yamtengo wina n’kunena kuti,<br />
“Musadzayerekezenso kumvera lonjezo limene munthu<br />
wogwidwa angadzakuuzeni, chimenechi ndi chinthu<br />
choyamba. Chachiwiri, osamataya kapena kusiya<br />
chinthu chokhacho chimene muli nacho ndipo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
130
chachitatu, osamakhalira kudandaula chinthu<br />
chimene ngakhale mutatani simungachipezenso.”<br />
Mbalameyo itangomaliza kunena zimenezi inauluka.<br />
Phunziro: Osalilira chinthu chimene palibe chomwe<br />
ungachite kuti uchipezenso. Osamada nkhawa ndi<br />
zinthu zimene sungazisithe chifukwa ungangotaya<br />
nthawi yako.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi ndi malangizo ati amene mbalame<br />
inapereka kwa munthu uja?<br />
2. N’chifukwa chiyani munthuyo analakwitsa<br />
kumvera zimene mbalameyo inamuuza?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
131
Nkhandwe, Nkhuku Komanso Galu<br />
Usiku wina Nkhandwe inkazemberera Nkhuku ndipo<br />
Nkhukuyo itazindikira zimenezi, inauluka n’kukwera<br />
mumtengo moti Nkhandweyo inkalephera kuigwira.<br />
Kenako Nkhandweyo inati, “Musaope a Nkhuku,<br />
ndabweratu kuti ndikuuzeni uthenga wabwino.<br />
Mfumu Mkango yalamula kuti pasapezekenso nyama<br />
yodya inzake kuyambira lero. Inati nyama zonse<br />
ziyenera kumakhala limodzi mogwirizana komanso<br />
mwamtendere.” Ndiyeno Nkhukuyo inati, “Uthenga<br />
wake ndi umenewo eti? Chabwino ndamva! Koma pali<br />
wina amene mwina mungakondenso mutamuuza<br />
uthenga umenewu. Mwina nayenso angasangalale<br />
ataumva.” Nkhukuyo inayamba kuyang’ana<br />
kunyumba komwe inkakhala. Ndiyeno Nkhandwe ija<br />
inafunsa kuti, “Kodi kukubwera chiyani?” Nkhukuyo<br />
inayankha kuti, “Kukubwera Galu wa mbuyanga.”<br />
Nkhandweyo itangomva zoti kukubwera galu,<br />
inatembenuka n’kuyamba kuthawa. Ndiyeno<br />
Nkhukuyo inauza nkhandwe ija kuti, “Kodi<br />
mungamuuzenso Galuyo uthenga mwabweretsa uja?”<br />
Koma Nkhandwe ija inati, “Ndikanakonda<br />
ndikanatero, koma ndikuopa kuti Galuyo akhoza<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
132
kundichita zoopsa chifukwa kunalibe pamene Mfumu<br />
Mkango imalengeza zoti pakhale mtendere wa zinyama<br />
zonse.” Nkhukuyo itamva zimenezi inamwetulira<br />
n’kunena kuti, “Nanga ine ndiye ndinaliko?”<br />
Phunziro: Bodza lili ngati matenda, ukhoza kuwabisa<br />
koma pamapeto pake ena amadziwa.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Nkhuku inadziwa bwanji kuti<br />
Nkhandweyo imanama?<br />
2. Kodi Nkhukuyi inaonadi galu wambuyake<br />
akubwera?<br />
3. Kodi ndi makhalidwe oipa ati amene Nkhandwe<br />
inasonyeza m’nkhaniyi?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
133
Munthu Wamanja Lende<br />
Munthu wina ankayendetsa ngolo yake atanyamula<br />
katundu wolemera m’nyengo ina yadzinja. Ngoloyo<br />
inkakokedwa ndi abulu awiri. Chifukwa choti kunali<br />
matope ambiri, matayala a ngoloyo analowa m’matope<br />
n’kutitimira. Ndiyeno munthuyo anayamba kumenya<br />
abulu akewo ndi chikwapu, koma sanakwanitse<br />
kuyenda. Kenako anatopa moti anataya chikwapucho<br />
n’kutsika pangoloyo. Ndiyeno anagwada pansi<br />
n’kupemphera kwa Mulungu kuti amuthandize. Anati,<br />
“Ambuye Mulungu, ndithandizeni chonde pa nthawi<br />
yovutayi.” Koma Mulungu anamuyankha kuti, “Ndiwe<br />
wopusa kwabasi! Tadzuka pamenepo ukakankhe<br />
ngolo yakoyo kuti ichoke m’matopemo!”<br />
Phunziro: Mulungu sangathandize munthu waulesi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
134
Mafunso<br />
1. Kodi tinganene kuti Mulungu anathandiza<br />
munthuyu? Ngati ndi choncho, n’chifukwa chiyani<br />
mwatero?<br />
2. Kodi Mulungu anauza munthuyo kuti achite<br />
chiyani?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
135
Bambo ndi Mwana Wake Apita Kumsika<br />
Bambo wina ankapita ndi mwana wake kukagulitsa<br />
bulu kumsika. Ndiyeno akuyenda kupita kumsikako,<br />
anakumana ndi munthu wina ndipo anawauza kuti,<br />
“Ndinu opusa kwambiri, bwanji osakwera buluyo?”<br />
Ndiyeno bamboyo anakweza mwana wakeyo pabuluyo<br />
n’kumapitiriza ulendo. Koma kenako anakumananso<br />
ndi gulu la anthu ndipo m’modzi mwa anthuwo anati,<br />
“Taonani mwana waulesiyu, iyeyo wakwera bulu koma<br />
bambo ake akuyenda wapansi!” Bamboyo atamva<br />
zimenezi anauza mwana wakeyo kuti atsike ndipo<br />
anakwerapo iyeyo. Koma asanapite patali anakumana<br />
ndi azimayi awiri ndipo m’modzi anawauza kuti,<br />
“Taonani bambo wopanda nzeruyu wakwera bulu,<br />
mwana wake akuyenda wapansi!” Zitatero, bamboyo<br />
anasowa chochita. Koma kenako anaganiza zoti<br />
angokwera pabuluyo limodzi ndi mwana wakeyo.<br />
Pamene ankachita zimenezi n’kuti atayandikira<br />
kumsika kuja ndipo anthu ena anayamba<br />
kuwalozerana n’kumawanena chipongwe. Bamboyo<br />
anatsika pabuluyo n’kuwafunsa kuti alakwa chiyani.<br />
Koma anthuwo anati, “Kodi mulibe manyazi thunthu<br />
lonselo komanso mwana wanuyo kukwera pamsana<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
136
pa bulu wamng’ono ngati ameneyu.” Bambo ndi<br />
mwana wakeyo sanakwerenso buluyo ndipo anaima<br />
kaye n’kuyamba kuganiza zoti achite. Pamapeto pake<br />
anaganiza zodula mtengo n’kumagirira buluyo<br />
n’kumunyamula pamapewa awo. Koma anadabwa<br />
kwambiri kuti anthu ankangowaseka ngati amisala<br />
ndipo posakhalitsa anafika pamlatho wolowera<br />
mumsika ndipo mwendo umodzi wa bulu uja<br />
unamasuka ndipo buluyo anagwa pansi n’kuthawa,<br />
moti sanakwanitsenso kumugwira. Ndiyeno munthu<br />
wina wachikulire, yemwe ankayenda pafupi nawo,<br />
anawauza kuti, “Mutengerepo phunziro, munthu<br />
amene amafuna kusangalatsa onse, sangasangalatse<br />
aliyense.”<br />
Phunziro: Sungakwanitse kusangalatsa aliyense.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani munthu ndi mwana<br />
wakeyu anamanga buluyo pamtengo?<br />
2. Kodi mawu akuti, “Munthu amene amafuna<br />
kusangalatsa onse, sasangalatsa aliyense”<br />
akutanthauza chiyani?<br />
3. Kodi pali nthano iliyonse imene munaimvapo<br />
imene mukuona kuti ikufanana ndi imeneyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
137
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
138
Munthu Woumira<br />
Kalekalelo panali munthu wina woumira kwambiri<br />
yemwe ankabisa ndalama zake pansi pamtengo<br />
wam’munda mwake. Mlungu ulionse ankapita<br />
pamtengopo n’kukumba ndalamazo, ndipo<br />
ankaziyang’ana kwinaku akunyadira kuti ali ndi<br />
ndalama zambiri. Koma tsiku lina wakuba anamuona<br />
akuchita zimenezi ndipo munthuyu atachoka,<br />
wakubayo anapita kukakumbapo ndalamazo<br />
n’kuthawa nazo. Ndiyeno munthuyu atapitanso kuti<br />
akaone ndalama zake, anapeza kuti zonse zabedwa.<br />
Zitatero anameta tsitsi lake ndipo anang’amba zovala<br />
zake n’kuyamba kulira koopsa. Anthu oyandikana<br />
nawo nyumba atamva kulirako, anabwera kuti<br />
adzaone chimene chachitika. Munthuyo<br />
anawafotokozera zonse zimene zinachitika. Anawauza<br />
kuti anakwirira ndalama zake pansi pamtengowo<br />
ndipo ankabwera mlungu ulionse n’kufukula<br />
ndalamazo moti akaziona mtima wake unkasangalala<br />
zedi. Anthuwo anamufunsa kuti, “Kodi munkatengako<br />
ndalama zina kuti mukagwiritse ntchito?” Munthuyo<br />
anayankha kuti, “Ayi, ndinkangobwera kuti<br />
ndidzazione basi. Ndinkamva bwino kwambiri<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
139
ndikaona ndalama zanga zochuluka.” Ndiyeno<br />
anthuwo anamuuza kuti, “Ndiyetu musasiye. Mlungu<br />
ulionse muzibwerabe pamtengopa ndipo<br />
muzingoyerekezera kuti ndalama zanuzo zidakalipobe.<br />
Zimenezi zikuthandizani kwambiri kuti muzisangalala.<br />
Si mwati munkangobwera kudzaziona?”<br />
Phunziro: Kukhala ndi ndalama kapena zinthu zambiri<br />
koma osamazigwiritsa ntchito, n’chimodzimodzi<br />
osakhala nazo.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani munthu woumirayu<br />
ankakumba ndalama zake nthawi zonse?<br />
2. Kodi akanatani kuti ndalama zake zisabedwe?<br />
3. Kodi akanakhala wanzeru akanachita chiyani<br />
ndi ndalama zakezo?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
140
Nkhandwe ndi Udzudzu<br />
Tsiku lina Nkhandwe inali paulendo ndipo itaoloka<br />
mlatho wina mchira wake unakodwa m’ziyangoyango<br />
moti inkalephera kuchoka. Udzudzu ungapo utaona<br />
zimenezi unakondwera kwambiri ndipo unayamba<br />
kuyamwa magazi a Nkhandweyo popanda<br />
kusokonezedwa ndi mchira wake. Kenako kunabwera<br />
Chisoni ndipo chinamva chisoni kwambiri ndi<br />
Nkhandweyo moti chinapita kuti chikaithandize.<br />
Chinauza Nkhandweyo kuti, “Kodi<br />
ndingakuthandizeko bwanawe pothamangitsa<br />
udzudzu ukukuyamwa magaziwu?” Koma<br />
Nkhandweyo inati, “Zikomo kwambiri pondiganizira<br />
achimwene anga a Chisoni. Koma musatero ayi. Si<br />
mwati mukufuna mungouthamangitsa?” Chisoni<br />
chinavomera ndipo chinafunsa kuti, “N’chifukwa<br />
chiyani simukufuna kuti ndiuthamangitse pomwe<br />
ukukuvutitsani?” Nkhandweyo inayankha kuti,<br />
“Udzudzuwu wangotsala pang’ono kukhuta, ndiye<br />
mukauthamangitsa ukaitana unzake wanjala<br />
kwambiri, moti ubwera n’kudzapopa magazi anga<br />
onse.”<br />
Phunziro: Kumaona patali.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
141
Mafunso<br />
1. N’chiyani chinachititsa kuti Chisoni chimvere<br />
chisoni nkhandwe?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inakana<br />
thandizoli?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
142
Nkhandwe Yopanda Mchira<br />
Tsiku lina mchira wa Nkhandwe unakodwa<br />
pamsampha ndipo pamene inkayesetsa kuti ichoke,<br />
mchirawo unaduka. Poyamba Nkhandweyo inkachita<br />
manyazi kupita pamene panali anzake poopa kuti<br />
azimuseka. Koma kenako inalimba mtima<br />
n’kukakumana ndi anzake onse n’kukawauza kuti<br />
akufuna kuwauza nkhani yofunika kwambiri.<br />
Nkhandweyo inauza anzakewo kuti nawonso adule<br />
michira yawo. Nkhandweyi inafotokoza kuti mchira si<br />
wabwino makamaka agalu akamakuthamangitsa.<br />
Inawafotokozeranso kuti ikunena zimenezo chifukwa<br />
imawaganizira komanso kuwakonda kwambiri.<br />
Inanena kuti sikufuna kuti anzakewo azinyamula<br />
pathupi lawo chinthu chomwe sichingawathandize,<br />
koma kungowabweretsera mavuto. Ndiyeno anzakewo<br />
anati, “Tamva ndithu bwanawe, amenewo ndi<br />
maganizodi abwino. Koma tikuona kuti iweyo<br />
sukanaganiza zotiuza kuti tidule michira yathu,<br />
yomwe ndi ziwalo zamtengo wapatali, zikanakhala kuti<br />
wako sunaduke. Tikuona kuti ukungofuna tifanane!”<br />
Phunziro: Osamakhulupirira malangizo ochokera kwa<br />
munthu amene alibe chimene uli nachocho.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
143
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkafuna kuti<br />
anzake adule michira yawo?<br />
2. Kodi tinganene kuti inkachita zimenezi<br />
powafuniradi zabwino?<br />
3. Kodi tingadziwe bwanji ngati munthu<br />
akutipatsadi malangizo chifukwa choti akutifunira<br />
zabwino?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
144
Kalulu wa Diso Limodzi<br />
Tsiku lina Kalulu anaphulika diso limodzi ndipo<br />
kungochokera pa tsikulo, zinkamuvuta kuona chinthu<br />
chimene chikubwera kuchokera mbali yomwe diso<br />
linaphulikayo. Ndiye pofuna kupewa mavuto,<br />
Kaluluyu ankakonda kudya pafupi ndi phompho lina<br />
lomwe kumunsi kwake kunali nyanja. Ankati<br />
akamadya diso lake labwinobwino lija linkakhala<br />
kumtunda, pomwe mbali inayo inkaloza kunyanja.<br />
Zimenezi zinkathandiza kuti aziona alenje<br />
akamabwera kudzamugwira ndipo nthawi zambiri<br />
ankathawa. Koma mlenje wina anatulukira kuti<br />
Kaluluyo analibe diso limodzi. Ndiye tsiku lina<br />
anakwera bwato n’kulowa m’nyanja, pansi pachitunda<br />
chomwe kalulu ankadyera paja. Kenako anakoka uta<br />
wake n’kubaya Kaluluyo. Kaluluyo analira kuti, “Mayo<br />
ineeeeeee! Zoonadi, imfa sithawika.”<br />
Phunziro: Ngakhale utayesetsa bwanji koma<br />
sungathawe imfa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
145
Mafunso<br />
1. Kodi Kalulu anatani kuti asaphedwe ndi<br />
mlenje?<br />
2. Kodi zimenezi zinathandizadi?<br />
3. N’chiyani chinachititsa Kaluluyu kuganiza kuti<br />
akamadyera malo amenewo akhala wotetezeka?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
146
Msonkhano wa Makoswe<br />
Kalekalelo, Mphaka wina ankavutitsa Makoswe<br />
kwambiri. Makoswewo anayamba kudandaula ndipo<br />
anapanga chimsonkhano cha mnzanga ali pati, kuti<br />
agwirizane zoti achite ndi mdani wawoyo. Atakumana,<br />
Khoswe wina wodziwa kuyankhula anaimirira<br />
n’kunena kuti, “Akuluakulu, Mphakayutu<br />
akutisowetsa mtendere, akutizunza kwabasi moti<br />
tikulephera kupeza chakudya choti tidyetse mabanja<br />
athu. Sindikudziwa kuti tipange bwanji ndi chipsinjo<br />
chatigwerachi?” Nkhaniyo inalowa m’bwalo ndipo<br />
makoswewo anayamba kupereka maganizo<br />
osiyanasiyana. Koma kenako, khoswe wina<br />
wamng’ono anaimirira n’kunena kuti, “Mphakayudi<br />
akutisowetsa mtendere. Mungandivomereze kuti<br />
mdani wathuyu amayenda mochenjera kwambiri moti<br />
umangozindikira wakugwira. Ndiye ngati titamamva<br />
phokoso lotichenjeza kuti akubwera, tikhoza<br />
kumamuzemba, ndipo palibe angagwidwe. Choncho<br />
maganizo anga ndi akuti tipeze belu n’kumumangirira<br />
m’khosi. Ndiyeno akamabwera, ifeyo tizimumva,<br />
tikamumva, tizithawa.” Anzakewo anasangalala<br />
kwambiri ndi mfundo anatsitsayi ndipo anayamba<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
147
kumuwombera m’manja kwinaku akuimba<br />
malikhweru. Kenako Khosweyo anakhala pansi<br />
akumwetulira ndipo ankaoneka kuti wakukhutira ndi<br />
zomwe wanena. Koma Khoswe wina wachikulire<br />
anaimirira n’kunena kuti, “Maganizowa ndi abwinodi.<br />
Koma kodi ndi ndani amene angalimbe mtima kuti<br />
akamuveke belu?” Makoswewo anayamba<br />
kuyang’anizana ndipo palibe anayankha. Kenako<br />
khoswe wachikulireyo anapitiriza kunena kuti, “Ndi<br />
ndani amene moyo sakuufuna? Maganizo ena<br />
amakhala abwino, koma si onse amakhaladi<br />
othandiza.”<br />
Phunziro: Si maganizo onse amene amakhaladi<br />
othandiza.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
148
Mafunso<br />
1. Kodi tinganene kuti maganizo oveka Mphaka<br />
belu, anali abwino kapena ayi? Ngati ndi choncho,<br />
n’chifukwa chiyani?<br />
2. Kodi mwina n’kutheka kuti Makoswe enawo<br />
ananena zotani zomwe zinali zosatheka kuthetsa<br />
vutolo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
149
Mpikisano wa Kalulu ndi Kamba<br />
Nthawi inayake Kalulu ankadzitama kuti ali ndi liwiro<br />
kuposa nyama iliyonse. Ankati, “Palibe anayambapo<br />
wandiposa kuthamanga. Ndikati ndiliyatse liwiro,<br />
ndimachita kukhala ngati mphenzi. Ndipo ndikhoza<br />
kukuuzani kuti panopa palibe amene angandipose<br />
kuthamanga. Ngati pali wina akutsutsa, abwere<br />
tipikisane.” Koma kenako Kamba anayankha kuti,<br />
“Chabwino, tiye tipikisane.” Kaluluyo atamva zimenezi<br />
anati, “Musandiseketse a Kamba! Zoona inuyoooo!<br />
Miyendo yake yolowa mkatiyi? Kayendedwe kanunso<br />
kamakhala ngati ka Mbozi, moti ndikhoza kukusiyani<br />
kuti muuyambe ineyo n’kupha kaye tulo. Kenako<br />
ndikhoza kudzuka, kukasamba, kudya, ndiyeno<br />
n’kuyamba kuthamanga, koma ineyo n’kukakhalabe<br />
woyamba kukafika.” Koma Kamba anati, “Ukhala<br />
chete pambuyo poti ndakuchotsa chimbenene. Tiye<br />
tipikisane!” Choncho anapangana mtunda woti<br />
athamange ndipo aliyense anakonzekera kuyambapo<br />
mpikisanowuo. Lipenga la mpikisanowo litangolira,<br />
Kalulu anatsomphoka ngati mwala walegeni ndipo<br />
posapita nthawi sanaonekenso. Koma<br />
atangothamanga pang’ono, anaima kaye kuti abe tulo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
150
pofuna kumutsimikizira Kamba kuti akucheperakaba.<br />
Kamba uja analimbikira kuthamanga moti pamene<br />
Kalulu ankadzuka, Kambayo anali akudutsa pamzere<br />
womaliza ndipo Kalulu sakanakwanitsa kuthamanga<br />
n’kumupitirira. Ndiyeno Kamba anati, “Munthu<br />
wakhama ndi amene amapambana mpikisano.”<br />
Phunziro: Munthu wakhama akhoza kuchita<br />
chilichonse.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi pakati pa Kalulu ndi Kamba<br />
chimathamanga kwambiri ndi chiyani? Ndiye<br />
n’chiyani chinapambana pampikisanowu, nanga<br />
n’chifukwa chiyani?<br />
2. Kodi pali zinthu zinanso zimene munthu<br />
amene amachita zinthu modekha komanso<br />
mosathamanga angapambane kuposa wachangu<br />
kwambiri?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
151
Gogo Akumana ndi Imfa<br />
Ukalamba umabwera ndi mavuto ambiri ndipo<br />
umapangitsa kuti moyo usamasangalatse. Ndiyeno<br />
kalekalelo, munthu wina anafika potopa ndi ukalamba<br />
chifukwa ankavutika kugwira yekha ntchito<br />
zapakhomo. Ngakhale kuyenda kumene kunkamuvuta<br />
kwambiri. Nthawi zonse ankangokhalira kudandaula<br />
msana, miyendo komanso kuphwanya kwa thupi. Kuti<br />
ayende, ankadalira mgongosera. Ndiye tsiku lina,<br />
anapita kunkhalango kukatola nkhuni zoti aphikire<br />
nandolo. Atamaliza kutola nkhunizo, anazimanga<br />
kamtolo ndipo anasenza n’kumapita kwawo. Koma<br />
kenako nkhunizo zinayamba kumugogoda ndipo<br />
anatopa kwambiri. Atalephera kupirira, anaponya<br />
mtolowo pansi n’kunena kuti, “Sindingakwanitse<br />
kupitirizabe kukhala moyo movutika chonchi!<br />
Ndikanakondwera imfa ikanangobwera<br />
kudzanditenga!” Nthawi yomweyo, imfa inatulukiradi<br />
ndipo inati, “Mayi, ndamva mukutchula dzina langa,<br />
mukundifuna eti? Tsopano ndabweratu, mukufuna<br />
ndikuchitireni chiyani?” Koma gogoyo anati,<br />
“Mwachitadi bwino kubwera. Kodi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
152
mungandithandizeko kusenza mtolowu? Ndikulephera<br />
kuusenza ndekha.”<br />
Phunziro: Zinthu zina zimene timafuna zitachitikadi,<br />
sitingazikonde n’komwe.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi munthu wokalambayu ankafunadi kufa?<br />
N’chifukwa chiyani mukutero?<br />
2. Kodi vuto lake linali chiyani kwenikweni?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
153
Kalulu ndi Anzake Ambirimbiri<br />
Kalulu anali nyama yotchuka kwambiri ndipo anali<br />
ndi anzake ambirimbiri. Koma tsiku lina anaona<br />
Nkhandwe zikubwera ndipo anaganiza zopempha<br />
anzakewo kuti amuthandize kuthawa. Ndiye anapita<br />
kwa Bulu n’kumupempha kuti amunyamule pamsana<br />
pake, koma Buluyo anakana ndipo anamuuza kuti<br />
mbuyake wamuuza kuti agwire ntchito inayake.<br />
Anamuuza kuti, “Ndikuganiza kuti utapempha<br />
Ng’ombe ikhoza kukuthandiza.” Kenako anapita kwa<br />
Ng’ombe akumaganiza kuti iopseza Nkhandwezo ndi<br />
nyanga zake. Koma ng’ombe nayonso inati, “Pepa<br />
m’bale wanga, ndinagwirizana ndi chibwenzi changa<br />
kuti tipite koyenda, ndiye ukudziwa kuti mnyamata<br />
safuna kukhumudwitsa njole yake! Ndikuganiza kuti<br />
utapempha Mbuzi ikhoza kukuthandiza mofanana ndi<br />
mmene ine ndikanachitira.” Koma atapitako, Mbuziyo<br />
inamuyankha kuti ikuvutika msana moti inadandaula<br />
kuti ngati itachita zimene amafunazo ndiye kuti sigona<br />
usiku, ingodziputira zina. Kenako inauza Kaluluyo<br />
kuti Nkhosa ikhoza kumuthandiza pa vuto lakelo<br />
ndipo anapitadi kwa Nkhosa. Koma Nkhosayo<br />
inamuuza kuti, “Ndikanakuthandiza m’bale wanga,<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
154
koma kungoti vuto lakoli landikulira. Ndakhala<br />
ndikumva kuti Nkhandwe zikumadya Akalulu ndi<br />
Nkhosa zomwe. Ndiye ndikuopa kuti nanenso<br />
ndikhoza kusiyana nalo dziko lapansi.” Kenako Kalulu<br />
anapita kwa mnzake womaliza amene ankaganiza kuti<br />
akhoza kumuthandiza. Mnzakeyo anali Tonde. Koma<br />
Tonde nayenso anakana kumuthandiza poganizira<br />
kuti anzake akuluakulu a Kaluluyo anali atakana<br />
kumuthandiza. Tonde ananena kuti kuvomera<br />
ntchitoyo chikanakhala chipongwe kwa nyama zinazo,<br />
zomwe zinali anzake aponda apo m’pondepo a<br />
Kaluluyo. Pa nthawiyi n’kuti Nkhandwe zija<br />
zitayandikira ndipo Kaluluyo anangoti, phazi thandize,<br />
ndipo mwamwayi anapulumukadi.<br />
Phunziro: Munthu amene ali ndi anthu ambirimbiri<br />
ocheza nawo sakhala ndi anzake enieni.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi nyama zomwe Kalulu ankaona kuti anali<br />
anzake apamtima, zinalidi anzake enieni?<br />
2. N’chifukwa chiyani nyamazi sizinkafuna<br />
kuthandiza Kalulu?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
155
Mkango Ugwa M’chikondi<br />
Nthawi ina Mkango unagwa m’chikondi ndi mtsikana<br />
wina wokongola kwambiri ndipo inapita kwa makolo<br />
ake kukafunsira ukwati. Koma anthu a kwawo kwa<br />
mtsikanayo sanadziwe choti anene. Iwo sankafuna<br />
kuti mwana wawo akwatiwe ndi Mkango. Komabe,<br />
ankaopa kuukwiyitsa. Ankadziwa kuti ngati atachita<br />
zinthu mosasamala akhoza kuphedwa. Kenako bambo<br />
a mtsikanayo anati, “Tikuona kuti ndi mwayi waukulu<br />
kuti mwabwera kwathu kuno kudzafunsira banja<br />
monga inuyo Mfumu ya Zinyama zonse. Koma tikuona<br />
kuti mwana wathuyu ndi wamng’ono kwambiri. Ndiye<br />
popeza muzikakhala naye, mukhoza kukamuvulaza<br />
ndi zala komanso mano anuwo. Ndiye timafuna<br />
tikupempheni kuti muwenge zala zanuzo komanso<br />
muzule mano anu akuluakuluwo. Kenako<br />
mudzabwere kudzatenga mtsikanayu kuti akhale<br />
mkazi wanu.” Popeza Mkangowo unakonda kwambiri<br />
mtsikanayo, unachitadi zimene makolowo anapempha.<br />
Unawenga zala zake komanso unachotsa mano ake<br />
akuluakulu. Koma utapita kwa makolo a mkazi uja,<br />
anthu anayamba kuuseka chifukwa cha mmene<br />
unkaonekera komanso chifukwa choti siunkaopsanso.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
156
Phunziro: Chikondi chikhoza kusintha munthu woopsa.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Mkango ukanatani kuti ukwatire<br />
mtsikanayo popanda kuwenga zala komanso<br />
kuchotsa mano ake?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti makolo a mtsikanayo<br />
analola kuti Mkango ukwatire mwana wawo,<br />
Mkangowo utawenga zala komanso kuzula mano<br />
ake? N’chifukwa chiyani mukutero?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
157
Kamtolo ka Mitengo<br />
Bambo wina anadwala kwambiri. Atatsala pang’ono<br />
kumwalira, bamboyo anaitanitsa ana ake kuti awauze<br />
mawu omaliza. Zimadabwitsa kuti anthu ambiri<br />
amadikira kaye kuti atsale pang’ono kutsirizika<br />
n’kumanena mawu omaliza, pomwe anali ndi nthawi<br />
yambirimbiri yoti akanachita zimenezo. Mwina<br />
amachita zimenezi popeza paja amati, mawu<br />
oyankhulidwa ndi munthu yemwe akutsirizika ndi<br />
omwe amatsakamira m’khutu. Ndiye bamboyu anauza<br />
wantchito wake kuti abweretse kamulu ka mitengo<br />
komwe anakamanga pamodzi ndipo anauza ana akewo<br />
kuti, “Tathyolani.” Mwana woyamba anayesetsa kuti<br />
athyole koma analephera. Mwana wachiwirinso<br />
anayesa koma analephera. Ndiyeno bamboyo anauza<br />
anawo kuti, “Tsopano masulani mitengoyo. Ndipo<br />
aliyense atenge kamtengo kamodzi.” Anawo atachita<br />
zimenezi, anawauza kuti, “Thyolani.” Anawo anathyola<br />
timitengoto mosavuta ndipo bamboyo anati, “Mwaona<br />
zimene zachitika? Mtengo suvuta kuthyola ukakhala<br />
wokha, koma ikakhala yambiri, imakhala yolimba<br />
kwambiri moti munthu sungaithyole. Nanunso<br />
muphunzirepo kanthu. Dziwani kuti ngati mutayamba<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
158
kukangana aliyense n’kuyamba kuchita zake, zinthu<br />
sizidzakuyenderani bwino. Nanunso mukapanda<br />
kusamala anthu adzakuthyolani ndipo mafupa anu<br />
adzalira gobedee!”<br />
Phunziro: Mu umodzi muli mphamvu.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi n’chifukwa chiyani zinali zophweka ana<br />
aja kuthyola mtengo umodziumodzi?<br />
2. Kodi tinganene kuti ana a bamboyu anali ngati<br />
mitengo imeneyi chifukwa chiyani?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
159
Mawu Omaliza a Mkango<br />
Nthawi ina Mkango unadwala mwakayakaya ndipo<br />
utatsala pang’ono kufa, unaitana nyama zonse kuti<br />
uziuze mawu omaliza. Unanena kuti izilowa nyama<br />
imodziimodzi kuphanga lake. Choncho Mbuzi inapita<br />
kuphanga la Mkango ndipo inamvetsera kwa nthawi<br />
yaitali mawu omaliza a Mkangowo. Kenako Nkhosa<br />
inakalowa ndipo kenako Ng’ombe nayonso inalowa<br />
kuti ikamve mawu omaliza a Mfumu ya Zilombo zonse.<br />
Phangalo silinkadziwika kuti ndi lalikulu bwanji<br />
chifukwa munali m’dima wa tsokomola<br />
ndingakuponde. Komabe nyamazo zinapitiriza kulowa<br />
m’phangalo. Koma kenako, Mkango uja unayamba<br />
kuchira moti unadzuka n’kuima pakhomo la phanga<br />
lake ndipo unaona Nkhandwe ikudikira panja pa<br />
phangalo. Ndiyeno unafunsa Nkhandweyo kuti,<br />
“N’chifukwa chiyani sukubwera kudzamva mawu anga<br />
omaliza?” Koma poyankha Nkhandweyo inati, “Pepani<br />
mfumu yanga, pansipa pakuoneka mapazi a nyama<br />
monga Mbuzi, Nkhosa komanso Ng’ombe, ndipo<br />
zikuoneka kuti nyamazi zalowa m’phanga lanulo.<br />
Koma sindikuona mapazi a nyamazi zikutuluka.<br />
Zimenezi zinandisokoneza mutu kwambiri, moti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
160
ndinayamba kuchita mantha. Mantha amenewa<br />
akhoza kutha ngati mutatulutsa nyama zonse zomwe<br />
zalowa m’phanga lanulo. Ngati mutatero ndiye<br />
mukhoza kundimasura moti nanenso ndikhoza<br />
kubwera kuti ndidzamve mawu anu omaliza.”<br />
Phunziro: N’zosavuta kugwera m’manja mwa adani<br />
koma zimakhala zovuta kutulukamo.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi chinachitika n’chiyani ndi nyama zomwe<br />
zinalowa m’phanga la Mkango lija?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti Mkango unkadwaladi?<br />
N’chifukwa chiyani mukutero?<br />
3. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkakayikira zoti<br />
Mkango umadwaladi mwakayakaya?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
161
Ubongo wa Mbawala<br />
Tsiku lina Mkango unagwirizana ndi Nkhandwe kuti<br />
zipite kosaka. Mkangowo unali utatumiza uthenga<br />
kwa Mbawala woiuza kuti nkhandwe ikufuna<br />
kukhazikitsa mtendere ndi Mbawalayo. Ndiyeno<br />
Mbawala itafika pamalo omwe anagwirizana kuti<br />
akakumane, inasangalala kwambiri kuona kuti<br />
Mkango nawonso wabwera monga mkhalapakati wa<br />
mgwirizanowu ndipo inaona kuti yalemekezedwa<br />
kwambiri ndi Mfumu ya Nyama zonse. Mbawalayo<br />
inati, “Ndafika kalekaletu pano, paja a mvula zakale<br />
anati kambalame kolawira ndi kamene kamatola<br />
mphutsi!” Nkhandwe itamva zimenezi inamwetulira<br />
n’kunena kuti, “Komatu khoswe wachiwiri ndi amene<br />
amadya zomwe zili pamsampha! Woyamba amafa<br />
atavuvutidwa ndi msamphawo.” Ali mkati<br />
mokambirana zimenezi, Mkango uja unagwira<br />
Mbawalayo n’kuipha ndipo unauza Nkhandwe ija kuti,<br />
“Chakudya chathu chalero ndi chimenechi. Ndikufuna<br />
kuti uziyang’anira nyamayi, ineyo ndikabe kaye tulo<br />
pang’ono. Ndiye popeza ukudziwa zimene ndimachita<br />
ndi anthu osamvera, usayerekeze n’komwe kukhudza<br />
nyamayi.” Mkangowo unachokadi ndipo Nkhandweyo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
162
inkayang’anira nyamayo. Koma patapita nthawi,<br />
Nkhandweyo inayamba kumva njala. Ndiye itaona kuti<br />
Mkango sukubwera, inaganiza zochotsa ubongo wa<br />
Mbawalayo n’kuudya. Posapita nthawi, Mkango uja<br />
unatulukira ndipo utayang’ana bwinobwino,<br />
unazindikira kuti ubongo wa Mbawalayo<br />
wachotsedwa. Kenako unafunsa Nkhandweyo<br />
mwaukali kuti, “Kodi iwee, ubongo wa nyamayi<br />
wausiya kuti?” Koma Nkhandweyo inayankha kuti,<br />
“Mbawalayitu inalibe ubongo, chifukwa ikanakhala<br />
kuti inali ndi ubongo, sikanabwera pano. Ikanayamba<br />
yaganiza kaye kuti chilengere Mulungu dziko,<br />
zinachitikapo liti Mbawala kupanga mgwirizano ndi<br />
Nkhandwe, mkhalapakati wakenso n’kukhala<br />
Mkango.”<br />
Phunziro: Munthu wanzeru sasowa choyankha.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi nzeru za Nkhandwe zinamuthandiza<br />
bwanji kudziwa zoyankha?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti Mkangowo<br />
unangoisiyasiya Nkhandweyo?<br />
3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
163
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
164
Nkhwazi Ibayidwa ndi Muvi<br />
Tsiku lina Nkhwazi inkauluka ndipo mwadzidzidzi<br />
inangozindikira kuti yabaidwa ndi muvi moti inavulala<br />
kwambiri. Kenako inayamba kugwa pansi ndipo<br />
magazi ankangoti chuuu kuchucha kuchokera<br />
pamene inabaidwapo. Itayang’ana pamene<br />
inabaidwapo inaona kuti muviwo unali<br />
utamangiriridwa ndi nthenga yake. Ndiye pamene<br />
inkafa inanena kuti, “Nthawi zambiri timapereka kwa<br />
adani athu chida choti atiphere.”<br />
Phunziro: Nthawi zina timapereka kwa adani anthu<br />
chida choti atiphere.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi ndi chiyani chimene mwina n’kutheka<br />
Nkhwazi inapereka kwa mdani wake chimene<br />
chinaiphetsa?<br />
2. Kodi mdani wa Nkhwaziyi ndi ndani?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
165
Kuwerengera Madzi a Mphutsi<br />
Tsiku lina mtsikana wina ananyamula mtsuko<br />
wodzadza ndi mkaka pamutu pake kuti akagulitse<br />
kumsika. Koma ali m’njira, anayamba kuganizira<br />
zomwe angachite ndi ndalama zomwe angapeze<br />
akagulitsa mkaka womwe anasenzawo. Anati,<br />
“Ndikakangougulitsa, ndikagula nkhuku kwa Angozo.<br />
Nkhukuzo zikakula, zidzayamba kuikira mazira<br />
ambirimbiri ndipo akadzachuluka, ndidzawagulitsa<br />
kwa a Nankhoma. Ndalama zomwe nditadzapeze<br />
ndikadzagulitsa mazirawo ndidzagula diresi yokongola<br />
komanso mpango woti ndizidzavala kumutu.<br />
Ndikuganiza kuti ndikamadzayenda nditavala<br />
zimenezi, anyamata onse azidzangondilondola.<br />
Sindikukayikira kuti Nachisale akadzaona zimenezi<br />
adzachita nsanje. Koma aa, ndizidzangokhala ngati<br />
sizikunditani, sindikundikhudzaaa!<br />
Ndizidzangomuyang’ana cham’mbali kwinaku<br />
ndikuyendetsa mutu wangawu chonchi . . . ” Nthawi<br />
yomweyo mtsuko unali pamutu uja unagwa pansi<br />
n’kusweka, ndipo mkaka wonse unataika. Zitatere<br />
anabwerera kwawo akulira n’kukawauza mayi ake<br />
zomwe zinachitika. Atamva zimene mwana wawoyo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
166
ananena, mayiwo anati, “Mwana wanga,<br />
osamawerengera zinthu zimene sunazipeze.”<br />
Phunziro: Osamawerengera madzi a mphutsi.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani mtsikanayu ankaganiza<br />
kuti mkaka wodzadza mtsukowo umuthandiza<br />
kuti adzagule diresi komanso mpango?<br />
2. Kodi akanatani kuti asagwetse mtsukowo?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
167
Hatchi ndi Bulu<br />
Tsiku lina Hatchi ndi Bulu zinkayendera limodzi.<br />
Hatchi inkayenda mwamatama pomwe Bulu anali<br />
atanyamula katundu wambirimbiri moti anali<br />
atalemedwa zedi. Bulu anadandaula kuti,<br />
“Ndimalakalaka ndikanakhala ngati iwe. Sugwira<br />
ntchito iliyonse, koma umapatsidwa zakudya zambiri<br />
komanso zonse zimaoneka kuti zimakuyendera<br />
bwino.” Ndiyeno tsiku lotsatira kunayambika<br />
nkhondo, ndipo Hatchiyo inatengedwa n’kupita<br />
kunkhondo moti ili kumeneko inavulala kwambiri<br />
n’kutsala pang’ono kufa. Bulu uja atamva zimene<br />
zinachitikazo anati, “Inetu ndimadzinamiza. Kuli<br />
bwino kumakhala movutika uli pamtendere kusiyana<br />
n’kumadya bwino moyo wako uli pachiswe.”<br />
Phunziro: Moyo ndi wofunika kwambiri kuposa<br />
chilichonse.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Bulu ankachitira nsanje<br />
Hatchi?<br />
2. Bulu ananena kuti Hatchi sinkachita<br />
chilichonse. Kodi ankanena zoona? Ngati<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
168
sankanena zoona, kodi Hatchi inkagwira ntchito<br />
yanji?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
169
Woliza Lipenga<br />
Tsiku lina munthu woliza lipenga kunkhondo<br />
anayandikira kwambiri adani ndipo anamugwira.<br />
Atangotsala pang’ono kumupha, munthuyo<br />
anapempha anthuwo kuti amuchitire chifundo. Anati,<br />
“Inetu sindimenya nawo nkhondo, ndipo sindinyamula<br />
chida chilichonse. Ndimangonyamula chitolilochi.<br />
Nanga chimenechi ndingaphere munthu ngati? Ndiye<br />
ndichitireni chifundo, musandiphe, chifukwa nanenso<br />
sindipha anthu!” Koma anthuwo anati, “N’zoona kuti<br />
sumenya nawo nkhondo, koma umalimbikitsa<br />
komanso kutsogolera asilikali kuti amenye nkhondo,<br />
ndiye tikupha pa chifukwa chimenechi.”<br />
Phunziro: Tikhoza osachita nawo zoipa, ngati zonena<br />
zathu zimalimbikitsa ena kuchita zimenezo,<br />
n’chimodzimodzi kuti nafenso timachita zinthuzo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
170
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani woliza lipenga ankaganiza<br />
kuti adani akewo samupha?<br />
2. Koma kodi woliza lipengayo akanapangitsa<br />
bwanji kuti adani akewo akumane ndi mavuto?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
171
Katswiri Wolira Nyama Zosiyanasiyana<br />
Pachikondwerero china, katswiri wina woyerekeza<br />
kulira kwa zinyama anaseketsa anthu kwambiri<br />
pamene ankalira nyama zosiyanasiyana. Pomaliza<br />
munthuyo analira ngati nkhumba ndipo anthu<br />
anasangalala kwambiri moti ankaganiza kuti ikulira<br />
ndi nkhumba yeniyeni. Ndiyeno munthuyo anaima<br />
kaye n’kunena kuti, “Kumeneku ndi kulira kwa<br />
nkhumba. Ngati mukukayikira kuti ndimaliradi ndi<br />
ineyo, mawa mudzakhale pomwepo kuti mudzamve<br />
kulira kwa nkhumba yeniyeni.” Anthuwo atamva<br />
zimenezi anaseka kwambiri ndipo tsiku lotsatira<br />
munthu uja anabweranso. Koma pa nthawiyi anabisa<br />
mwana wankhumba ndipo anawerama<br />
n’kumamukoka khutu. Mwana wankhumbayo<br />
anayamba kulira ndipo anthuwo atamva kulirako<br />
anayamba kumugenda n’kumauza munthuyo kuti<br />
asiye. Munthuyo anati, “Ndinu wopusa kwabasi.<br />
N’chifukwa chiyani mumasangalala munthu<br />
akamayerekeza kulira kwa nyama n’kumadana ndi<br />
kulira kwa nyama yeniyeniyo?”<br />
Phunziro: Anthu amasangalala ndi kuyerekezera<br />
chinthu chinachake n’kumadana ndi chinthucho.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
172
Mafunso<br />
1. Kodi katswiriyu ankapanga chiyani chomwe<br />
chinkaseketsa anthu?<br />
2. N’chifukwa chiyani anthu aja anakwiya ataona<br />
kuti imene imalirayo inali nkhumba yeniyeni?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
173
Nkhandwe ndi Mbuzi<br />
Tsiku lina Nkhandwe inkayendayenda m’nkhalango<br />
ndipo mwatsoka inagwera m’mbuna ndipo inkalephera<br />
kutulukamo. Ndiyeno zinachitika kuti Mbuzi<br />
inkadutsa pafupi ndi mbunayo ndipo Mbuziyo itaona<br />
Nkhandweyo inafunsa kuti, “Kodi mukutani<br />
m’menemo?” Nkhandweyo inayankha kuti, “Chaka<br />
chino kukhala chilala choopsa moti madzi azisowa.<br />
Ndiye ndikukumba chitsimechi kuti chilalacho<br />
chikamafika, ndikhale ndili ndi madzi okwanira.<br />
Nawenso dumphira momwemuno tithandizane kuti<br />
tizidzamwera limodzi madziwa.” Mbuziyo itamva<br />
zimenezi inaona kuti umenewo ndi mwayi wake, moti<br />
inalumphiradi m’mbunamo. Kenako Nkhandwe ija<br />
inalumphira pamsana pambuziyo n’kutuluka<br />
m’dzenjemo ndipo inati, “Tionana bwanawe.<br />
Kuyambira lero usadzayerekezenso kumvera<br />
malangizo ochokera kwa munthu yemwe wapanikizika<br />
ndi mavuto.”<br />
Phunziro: Osamakhulupirira malangizo ochokera kwa<br />
munthu amene wapandikizika, akhoza kukhala kuti<br />
akungofuna njira yothawira mavutowo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
174
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Mbuzi inadumphira<br />
m’dzenje muja?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkafuna kuti<br />
Mbuziyo igwere m’dzenjemo?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
175
Nsikidzi ndi Ana Ake<br />
Munthu wina atatopa kulumidwa ndi Nsikidzi,<br />
anaganiza zotereka madzi kuti azikhaulitse. Kenako<br />
anatenga bulangete lakelo n’kuliika munkhali<br />
n’kutenga madzi obwadamuka n’kuwakhuthulira<br />
momwe munali bulangetelo kuti nsikidzizo zikhaule.<br />
Ndiye zimenezi zitangochitika, Nsikidzi yomwe inali<br />
m’bulangetemo inauza ana ake kuti, “Ana anga,<br />
muyenera kukhala opirira, chifukwa chilichonse<br />
chotentha, pamapeto pake chimazizira. Vuto<br />
lingatenthe bwanji, limakhala ndi mapeto ake.”<br />
Phunziro: Chilichonse chotentha, pamapeto pake<br />
chimazizira. Mavuto angakule bwanji, amakhala ndi<br />
polekezera.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi munthu anatani Nsikidzi zitamuvuta zedi?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nsikidzi inauza ana ake<br />
kuti “chilichonse chotentha, pamapeto pake<br />
chimazizira”?<br />
3. Kodi ndi zoona kuti vuto lililonse limakhala ndi<br />
pothera?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
176
Nyani ndi Mwana Wake<br />
Nthawi inayake, padziko lapansi panachitika<br />
mpikisano woonetsa ana okongola kwambiri. Ndiye<br />
Nyani atangomva za mpikisanowu, nayenso anatenga<br />
mwana wake n’kuthamangira komweko. Malamulo a<br />
mpikisanowo anali akuti, usanayambe kuchita nawo<br />
mpikisanowo unkafunika kukaonetsa mwana wako<br />
kwa wochititsa mpikisanowo. Ndiye wochititsa<br />
mpikisanowo ataona mwana wa Nyaniyo anaseka<br />
koopsa, ndipo anafunsa Nyaniyo kuti, “Mayi,<br />
mwabweretsachi n’chiyani?” Nyaniyo anayankha kuti,<br />
“Mwana, bwanji?” Wochititsa mpikisanowo anati,<br />
“Nanga bwanji mphunozi?” Akuti ankaseka mphunozo<br />
chifukwa zinkangooneka ngati zochita kuboola ndi<br />
tchizulo. Kenako anapitirizabe kuseka mwachipongwe<br />
kwambiri. Koma kenako Nyaniyo anati, “Inuyo<br />
mukhoza kuseka mmene mungathere. Koma dziwani<br />
kuti kwa ineyo, padziko lonse lapansili palibenso<br />
mwana wina wokongola kwambiri kuposa wangayu!”<br />
Phunziro: Mwana sanyansa mayi wake. Anthu ena<br />
akhoza kumamuona kuti ndi wonyansa, koma kwa<br />
mayi wake ndi wokongola kwambiri.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
177
Mafunso<br />
1. Kodi tinganene kuti Nyani ankaonadi kuti<br />
akhoza kupambana mpikisanowo?<br />
2. N’chifukwa chiyani wochititsa mpikisanowu<br />
anaseka ataona mwana wa Nyaniyo?<br />
3. Kodi nyaniyo anayankha zotani?<br />
4. Kodi wochititsa mpikisanowu analakwitsa<br />
chiyani?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
178
Nkhuku ndi Mwala Wamtengo Wapatali<br />
Tsiku lina Tambala ankayendayenda kwinaku<br />
akusaka chakudya. Kenako anafukula kanthu<br />
kenakake kowala pakati pazinyalala. Ndiyeno anati,<br />
“Ho! ho! Mulungu sapatsa pamanja!” Kenako<br />
anakachotsa pazinyalalapo ndipo anazindikira kuti ndi<br />
kamwala kamtengo wapatali. Ndiyeno anati, “Ukhoza<br />
kukhaladi wamtengo wapatali kwa anthu amene<br />
amakuona ngati mwala wapadera. Koma kwa ineyo,<br />
chinthu chamtengo wapatali ndi deya kapena misere<br />
imene imandithandiza kuti ndikhale ndi moyo!”<br />
Phunziro: Chinthu chimakhala chamtengo wapatali<br />
malinga ndi mmene munthu akuchionera.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mukuganiza kuti tambala ankaganiza kuti<br />
wapeza chiyani?<br />
2. Kodi chinthu chamtengo wapatali chimene<br />
tambalayu ankafunafuna chinali chiyani?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
179
Khoswe ndi Msampha<br />
Bambo wina makoswe anamuvuta zedi ndipo amati<br />
akagula chinthu, Makoswewo ankamubera<br />
n’kukalowetsa kuuna wawo. Tsiku lina makoswewo<br />
anamusautsa kwambiri chifukwa<br />
ankaongoyendayenda padenga moti tulo sadatione.<br />
Zinafika pomukwana kwambiri Makoswewo<br />
atamuboolera zovala zake ndipo anaganiza zothana<br />
nawo. Anayesa kuwathirira tameki, koma palibe ndi<br />
m’modzi yemwe amene anadya. Kenako anaganiza<br />
zotchera misampha. Anaika misampha ingapo<br />
m’nyumbamo ndipo pamsampha uliwonse anaika<br />
chakudya chomwe Makoswewo ankachikonda<br />
kwambiri. Makoswewo ataona zimenezi, anakopeka<br />
kwambiri moti khoswe wina anati, “Tiyeni<br />
tikasangalale ndi chakudya!” Koma mnzake anamuuza<br />
kuti, “Taima kaye bwanawe, wadziwa bwanji kuti<br />
tikasangalala. Kodi munthuyu anayamba wachitazo<br />
zimenezi? Mwinatu akufuna atikole.” Koma Khoswe<br />
wina wadyera kwambiri sanaupeze mtima, moti<br />
anaganiza zotenga chakudya chomwe chinali<br />
pamsampha wina. Atangochigwira, msamphawo<br />
unafwamphuka ndipo unamukang’antha pamimba.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
180
Khosweyo anayamba kulira ndipo anauza anzakewo<br />
kuti, “Chakudyachi ndilibe nachonso ntchito,<br />
mukhoza kuchitenga. Chomwe ndikufuna panopa ndi<br />
kuchoka pamsamphawu.”<br />
Phunziro: Kumaganizira zotsatira za zomwe<br />
mukuchita. Osamangotengeka ndi chilichonse.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi khoswe wadyera anatengeka ndi chiyani?<br />
2. Kodi ananena chiyani atapanidwa ndi<br />
msampha?<br />
3. Kodi tinganene kuti sankachifunadi<br />
chakudyacho? N’chifukwa chiyani anasintha<br />
maganizo?<br />
4. N’chifukwa chiyani tiyenera kumaganizira<br />
mavuto amene tingakumane nawo tisanachite<br />
chilichonse?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
181
Nkhani ya Kutha kwa Dziko<br />
Kagiso anali ndi mbuzi ndipo pa nthawiyi n’kuti<br />
itakula ndithu. Ndiye tsiku lina kunabwera anzake<br />
omwe ankakhala moyandikana nawo nyumba<br />
n’kumuuza kuti aphe mbuziyo. Atawafunsa chifukwa<br />
chake, anthuwo anamuuza kuti, “Nkhosa yakoyitu<br />
yanenepa. Tiye tikaiphe kumtsinje. Popeza kunjaku<br />
kwatentha, tikaiphere kumtsinjeko kuti<br />
tikakatenthedwa tizikangolowa mumtsinje<br />
n’kumasambira.” Koma Kagiso anawayankha kuti,<br />
“Ayi, sindikufuna kupha mbuzi yanga.” Koma wina<br />
anamuuza kuti, “Kodi sunamve? Dzikolitu likutha<br />
mawa!” Kagiso anadabwa ndi zimenezi ndipo ataona<br />
kuti akhoza kufa asanadye mbuzi yake, anavomera<br />
zoipha ndipo anaigwira n’kumapita nayo kumtsinje.<br />
Atafika kumeneko anaipha ndipo anayamba kuisenda<br />
chikopa. Anzake aja atayamba kumva kutentha<br />
anavula zovala zawo zonse n’kuyamba kusambira.<br />
Koma Kagiso ankangoti jijirijijiri kukonza mbuzi ija.<br />
Atamaliza kuikonza, anakoleza moto ndipo anayamba<br />
kuiwotcha. Pa nthawiyi n’kuti anzake aja akupanga<br />
chipako cham’madzi. Patapita nthawi, kafungo<br />
kabwino kanayamba kumveka ndipo anzake aja<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
182
anatuluka m’madzi muja n’kumuuza kuti, “Koma<br />
ndiye utipha ndi fungotu, tigawireko titsuke<br />
m’kamwa.” Koma atayang’ana pamene panali zovala<br />
zawo anaona kuti palibe ndipo anamufunsa kuti,<br />
“Kodi zovala zathu wazisiya kuti?” Kagiso anayamba<br />
kuzimbaitsa nkhaniyi amvekere, “Inetu ndimadabwa<br />
anthu akamanena kuti zovala. Ndimaona kuti munthu<br />
akavula zimene anavala n’kuziika poteropo,<br />
sizikhalanso zovala, koma zovula.” Anzakewo atamva<br />
zimenezi anakwiya kwambiri ndipo anamuuza kuti,<br />
“Usatitayitse nthawi iweeee! Zovala zathu wazisiya<br />
kuti?” Ndiyeno Kagiso anayankha kuti, “Ndazikolezera<br />
moto!” Atamva zimenezo anzakewo anapsa mtima<br />
kwambiri ndipo anati, “Zoona ungakolezere moto<br />
zovala zathu?” Koma Kagiso anayankha kuti, “Ee, pali<br />
vutoo? Si paja munati dziko likutha mawa, ndiye<br />
mukufunanso zovala zantchito yanji?” Anzakewo<br />
anangoti kukamwa yasaa, ndipo anayamba kuganizira<br />
mmene angayendere kuti akafike kwawo.<br />
Phunziro: Nthawi zina ukamapusitsa mnzako,<br />
umakhalanso ukudzipusitsa wekha.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
183
Mafunso<br />
1. Kodi zimene anzake a Kagiso ankanena, zoti<br />
dziko likutha mawa, zinali zoona? N’chifukwa<br />
chayani mukutero?<br />
2. N’chifukwa chiyani Kagiso anakolezera moto<br />
zovala za anzakewo?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
184
Nkhani ya Kalulu ndi Nkhandwe Yatulo<br />
Iyi ndi nkhani ya achikulire a Kalulu ndi Nkhandwe.<br />
Tsiku lina Kalulu ankafuna kupusitsa Nkhandwe<br />
ndipo anaima pafupi ndi mwala wina. Mwalawo<br />
unaima ngati ukufuna kugwa ndipo Kalulu<br />
ankaukankhira m’mwamba. Nkhandwe itaona<br />
zimenezi inafunsa Kalulu kuti, “Achikulire, mukutani<br />
pamenepo?” Ndiyeno Kalulu anaiuza kuti, “Tabwera<br />
mwamsanga bwanawe, mwalawutu ukugwa. Taugwira<br />
kuti ineyo ndikatenge mtengo tidzauimikire.”<br />
Nkhandweyo inavomeradi ndipo Kaluluyo<br />
ananyamuka n’kumapita n’kuisiya Nkhandwe itagwira<br />
mwalawo. Nkhandweyo inachita zimenezi kwa nthawi<br />
yaitali zedi koma Kalulu uja sanabwererenso.<br />
Nkhandweyo inayamba kuitana Kalulu uja ndipo<br />
inkati, “Kodi simunaupezebe mtengowo, mwalawutu<br />
ukundilemera.” Koma kunali zii. Nkhandweyo<br />
itatheratu, inaganiza zosiya mwalawo. Inausiya<br />
mwachanguchangu n’kuchokapo kuti usaigwere.<br />
Koma itachoka, inaona kuti mwalawo sunasunthe.<br />
Ngakhale inaona zimenezi, Nkhandweyo sinatengerepo<br />
phunziro. Tsiku linanso Kalulu anapita kukamwa<br />
madzi padziwe lina ndipo m’madzi munkaoneka<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
185
mwezi. Apa anaganizanso zopusitsa Nkhandwe ija<br />
ndipo anaiitana n’kuiuza kuti, “Taona m’madzimo,<br />
pansi pamadzipo, chimenechotu ndi chakudya.”<br />
Ndiyeno Nkhandweyo inati, “Ee, ndachiona, ndi<br />
chakudya chanji?” Kaluluyo anayankha kuti, “Ndi<br />
mtanda wa nsima. Kuteroko ineyo ndayamba kale<br />
kumwa madziwa n’cholinga choti aphwe. Ndiye popeza<br />
ndiwe wamkulu, ukhoza kumaliza madzi atsalawa,<br />
kuti kenako titenge nsimayo tidye. M’bale wanga,<br />
tamwa madziwa kuti timeze kadaunda madzi.”<br />
Nkhandwe yatuloyo inavomeranso zimenezi ndipo<br />
inayamba kumwa madzi aja. Sinazindikire kuti<br />
chimene chimaoneka m’madzicho si nsima koma<br />
mwezi. Kenako kalulu uja anatsanzika n’kumapita.<br />
Nkhandweyo inamwa madziwo mpaka mimba yake<br />
inangoti nguu, kukhuta. Itaona kuti sakuthapo,<br />
inangonyamuka n’kumapita kwawo ndipo usiku wa<br />
tsiku limenelo sinatione tulo chifukwa cha kupweteka<br />
kwa mimba yake.<br />
Phunziro: Osalola kuti munthu akupusitse kawiri.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
186
Mafunso<br />
1. Kodi Kalulu anapusitsa bwanji Nkhadwe?<br />
2. N’chiyani chikusonyeza kuti Nkhandweyo inali<br />
yatulo?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
187
Anyamata Awiri Akumana ndi Wokalamba<br />
Kalekalelo panali anyamata awiri a pachibale.<br />
Anyamatawa anaganiza zoyamba kuyendayenda<br />
padzikoli kuti akafunefune mwayi komanso<br />
chisangalalo. Ali m’njira anaona bambo wina<br />
wachikulire akuyenda patsogolo pawo. Bamboyu anali<br />
ndi ndevu zowirira zedi. Ndiyeno mnyamata wamkulu<br />
anati, “Wamuona bambo uyo? Alitu ndi ndevu zoti<br />
ndikhoza kuzendewera. Ndevu zopangitsa mwana<br />
kufunsa kuti, ‘Ababa pakamwa mpati?’ Mwina<br />
mwachidule ndingoti ali ndi ndevu za ponya mtedza<br />
upaone.” Anyamatawo ankachita chidwi ndi ndevuzo<br />
moti bamboyo anaima n’kuwafunsa kuti, “Mukupita<br />
kuti?” Anyamatawo anamufotokozera chimene<br />
ankafuna ndipo bamboyo anati, “Ndikhozatu<br />
kukuthandizani.” Kenako anapisa m’thumba<br />
n’kutulutsa kajumbo kodzadza ndi ndalama. Kenako<br />
anafunsa anyamatawo kuti, “Ndani amene akufuna<br />
ndalamazi?” Nthawi yomweyo mnyamata wamkulu uja<br />
anayankha kuti, “Ndipatseni ine!” Bamboyo<br />
anamupatsadi ndipo kenako anapisanso m’thumba<br />
n’kutulutsa mwala wamtengo wapatali ndipo<br />
anafunsaso kuti, “Ndani akufuna mwala wamtengo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
188
wapataliwu?” Nthawi yomweyo mnyamata wamkulu<br />
uja anayankhanso kuti, “Ndipatseni ine!” Bamboyo<br />
anamupatsadi. Koma mnyamata wamng’ono uja<br />
sanalandire kanthu. Ndiyeno bambo wachikulireyo<br />
anatula thumba limene ananyamula n’kupempha<br />
anyamata awiriwo kuti, “Ndani amene<br />
atandinyamulire thumbali kuti akandisiyire kwathu?”<br />
Atamva zimenezi, mnyamata wamkulu uja anangoti<br />
duu. Koma wamng’ono uja anapinda malaya ake<br />
n’kusenza thumbalo n’kuuza munthu wachikulireyo<br />
kuti, “Tiyenitu muzinditsogolera.” Bamboyo<br />
anangomwetulira n’kumuuza kuti, “Tenga thumbali<br />
mwana wanga, ndakupatsa kuti likhale lako.<br />
Utengenso zonse zimene zili mkatimo.” Mnyamatayo<br />
atamva zimenezo anati, “Ayi, musatero, ndikungofuna<br />
kukuthandizani basi.” Koma bamboyo anamuuza kuti<br />
wamupatsa monga mphatso. Mnyamatayo atatsegula<br />
thumbalo, sanakhulupirire zimene anaona. Anapeza<br />
kuti thumbalo linali lodzadza ndi miyala yamtengo<br />
wapatali!<br />
Phunziro: Khalidwe labwino ndi limene limapangitsa<br />
munthu kupeza mwayi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
189
Mafunso<br />
1. Kodi anyamata awiriwa ankafuna chiyani?<br />
2. Kodi anyamatawa anali osiyana bwanji?<br />
3. Ndi uti amene anali wakhalidwe labwino?<br />
N’chifukwa chiyani mukutero?<br />
4. Kodi khalidwe labwino linathandiza bwanji<br />
mnyamata wamng’ono uja kupeza mwayi<br />
waukulu?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
190
Chisoni Chinapha Nkhwali<br />
Kalekalelo Njoka inkafuna kuwoloka mtsinje wina.<br />
Ndiye popeza palibe chimene ikanachita kuti iwoloke<br />
yokha, inapempha Nkhwali kuti aithandize. Nkhwaliyo<br />
inamva chisoni zedi ndi mmene Njokayo inkaonekera<br />
ndipo inavomera kuti ichitadi zimene Njokayo<br />
inkafuna. Inauza Njokayo kuti, “Zizengereze m’khosi<br />
mwangamu!” Kenako inanyamuka n’kuuluka. Itafika<br />
kutsidya, Nkhwaliyo inauza Njokayo kuti, “Bwanawe,<br />
tafikatu. Tsopano ukhoza kutsika kuti uzipita.” Koma<br />
Njokayo inakana kwamtuwagalu kuti sichoka.<br />
Pamapeto pake, chisoni chinachitsa kuti Nkhwali ione<br />
tsoka la nkhuku.<br />
Phunziro: Chisoni nthawi zina chimapweteketsa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
191
Mafunso<br />
1. N’chiyani chinachititsa kuti njoka ipemphe<br />
thandizo kwa nkhwali<br />
2. Kodi njokayo inayamikira zimene mnzakeyo<br />
anamuchitira?<br />
3. N’chifukwa chiyani tinganene kuti nkhwali<br />
sinaganize bwino povomera kuthandiza njoka?<br />
4. Kodi nkhwali inakumana ndi zotani pamapeto<br />
pake?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
192
Chisoni Chinaphetsa Wosema Mitondo<br />
Nthawi ina alenje anavumbulutsa gondwa ndipo<br />
anayamba kumuthamangitsa. Alenjewo<br />
anamupezeketsa gondwayo moti anangotsala pang’ono<br />
kumugwira. Gondwayo anayesetsa kukoka phazi<br />
koma sizinam’thandize moti anaganiza zopempha<br />
thandizo kwa munthu wina yemwe ankasema mitondo<br />
m’nkhalangomo. Atatoperatu, gondwayo anapempha<br />
wosema mitondoyo kuti, “Ndithandizeni chonde<br />
ndagwira mwendo wanu. Alenjewa akufuna moyo<br />
wanga, chonde ndipulumutseni!” Wosema mitondoyo<br />
anamva chisoni kwambiri ndipo anauza Gondwayo<br />
kuti amubisa. Koma popeza panalibe malo pafupi<br />
pomwe akanamubisapo, wosema mitondoyo<br />
anangoganiza zomubisa m’kamwa. Alenjewo atafika<br />
anafunsa wosema mitondoyo kuti, “Mwaona Gondwa<br />
atadutsa apa?” Koma wosema mitondoyo anapukusa<br />
mutu posonyeza kuti sanamuone. Ndiyeno alenjewo<br />
atachoka, munthuyo anauza Gondwa uja kuti, “Alenje<br />
ajatu apita, ukhoza kutuluka tsopano!” Koma<br />
gondwayo anayankha kuti, “Tadikirani kaye pang’ono,<br />
muli kenakake kokoma muno!”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
193
Phunziro: Kumaona anthu owathandiza, ena akhoza<br />
kungokubweretsera mavuto.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani wosema mitondo anaganiza<br />
zothandiza Gondwa?<br />
2. Kodi Gondwa anayamikira zimene munthuyo<br />
anamuchitira?<br />
3. Mukuganiza kuti chinamuchitikira munthuyu<br />
n’chiyani?<br />
4. Kodi nthanoyi ikufanana bwanji ndi ya mutu<br />
wakuti, “Chisoni Chinaphetsa Nkhwali”?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
194
Azimayi Anzeru<br />
Kalekalelo, mfumu ina yamphamvu kwambiri inalanda<br />
mzinda wina. Mfumuyi inalamula kuti amuna onse a<br />
m’mudziwo aphedwe, koma akazi anauzidwa kuti<br />
akhoza kuthawa. Anauzidwanso kuti akhoza kutenga<br />
chilichonse chimene angakwanitse kunyamula.<br />
Azimayiwa atamva izi, anangolowa m’nyumba zawo<br />
n’kukaika amuna awo kumbuyo n’kumathawa nawo.<br />
Mfumuyo itaona zimenezi inafunsa azimayiwo kuti,<br />
“N’chifukwa chiyani mukuchita zimenezi? Si paja<br />
ndinakuuzani kuti muthawe nokha?” Koma azimayiwo<br />
anayankha kuti, “Pajatu munati tikhoza kutenga<br />
chilichonse chimene tingakwanitse kunyamula! Ndiye<br />
kwa ifeyo katundu ofunika kwambiri ndi amene<br />
tanyamulayu!” Mfumuyo inaona kuti zimenezi<br />
n’zomveka, moti inalola azimayiwo kutenga katundu<br />
ananyamulayo, ndipo amuna onse a m’mudziwo<br />
anapulumuka.<br />
Phunziro: Osamaiwala zinthu zofunika kwambiri.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
195
Mafunso<br />
1. N’chiyani chikusonyeza kuti azimayiwa anali<br />
anzeru?<br />
2. Kodi ndi zinthu zina ziti zimene akanakwanitsa<br />
kunyamula, kupatulapo amuna awo?<br />
3. Kodi anagwiritsa ntchito bwanji mawu a<br />
mfumu kupulumutsa amuna awo?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
196
Mwana Wosamvera<br />
Mayi wina anali ndi mwana wosamvera, mwanayu<br />
sankamva ndi pakamwa pokha, koma am’menye basi.<br />
Nthawi zina amati akamuuza kuti asachite zinazake,<br />
ankakhala ngati wamva, koma zomwe ankachita<br />
pambuyo pake, zinkasonyeza kuti zimene wauzidwazo<br />
zangolowera khutu ili n’kutulukira linalo. Ndiye tsiku<br />
lina mayiyo anauza mwanayo kuti, “Kunjatu kwacha<br />
kalekale, nyamuka uzipita kusukulu, ukachedwatu<br />
aphunzitsi akakubweza!” Koma mwanayo sanamvere<br />
ndipo anapitirizabe kumuuza kambirimbiri, koma ayi<br />
ndithu ankangozikankhira kunkhongo. Ankachita<br />
zinthu ngati kuti kusukuluko ankakaphunzirira mayi<br />
akewo. Koma akakhalanso pakhomo ankawatopetsa<br />
mayi ake chifukwa ankakana kugwira ntchito.<br />
Chinthu chimene ankachidziwa kunali kudya basi.<br />
Ndiye mayiyu atatopa ndi khalidwe la mwanayu,<br />
ananyamuka n’kupita kwa a Chikwapu. Atafika<br />
anawauza kuti, “Mwana wanga akuvuta, kodi<br />
mungakamukwapule kuti apite kusukulu?” Koma a<br />
Chikwapu anakana. Zitatero mayiyo anaganiza zopita<br />
kwa a Moto. Anawafotokozera kuti akufuna kuti a<br />
Motowo akawotche a Chikwapu chifukwa akukana<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
197
kukakwapula mwana, ndipo mwana akukana kupita<br />
kusukulu. Koma nawonso a Moto anakana. Mayiyo<br />
anakhumudwa kwambiri ndi zimenezi moti anaganiza<br />
zopita kwa a Madzi. Atafika kumeneko<br />
anawafotokozera kuti, “Pepanitu a Madzi. Ineyo<br />
ndikufuna thandizo lanu. Ndikufuna mukazimitse a<br />
Moto chifukwa akukana kuwotcha a Chikwapu, a<br />
Chikwapu akukana kukwapula mwana, mwana<br />
akukana kupita kusukulu.” Koma nawonso a Madzi<br />
anakana. Kenako mayiyo anapita kwa a Ng’ombe.<br />
Anawafotokozeranso nkhani yonse koma nawonso<br />
anakana. Zitatero, anaganiza zopita kwa M’busa<br />
wang’ombe. M’busayo anawamvetsa mayiwa chifukwa<br />
nawonso anali ndi mwana wovuta ndipo ananyamuka<br />
n’kuyamba kuthamangitsa a Ng’ombe. A Ng’ombe<br />
ataona kuti zavuta, anayamba kuthamangira kumene<br />
kunali a Madzi. A Madzinso ataona kuti amwedwa,<br />
anaganiza zokazimitsa a Moto. A Moto ataona kuti<br />
azimitsidwa, anaganiza zokawotcha a Chikwapu.<br />
Ndipo a Chikwapu ataona kuti zinthu sizili bwino,<br />
anayamba kukwapula mwana ndipo mwana anapita<br />
kusukulu.<br />
Phunziro: Osamamva nkhwangwa ili m’mutu.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
198
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani mwana ankakana kupita<br />
kusukulu?<br />
2. Kodi zimene ankachitazi zikanakhudza bwanji<br />
tsogolo lake?<br />
3. N’chiyani chinachititsa kuti apite kusukulu?<br />
4. Kodi nkhaniyi ikusonyeza kuti kulanga mwana<br />
n’kofunika bwanji?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
199
Mwana Wamwano<br />
Pamudzi wina panali mwana wosamvera komanso<br />
waulesi. Makolo ake amati akamutuma ankakana, apo<br />
ayi ankangochokapo n’kupita kukabisala. Ndiye tsiku<br />
lina anamukakamiza kuti apite kumunda ndipo<br />
atafika kumundako, mwanayo anakwera mumtengo<br />
n’kubisala. Mumtengomo munali njoka ndipo njokayo<br />
inamuluma moti anafera pompo. Makolo ataona kuti<br />
mwana wawo sakuoneka, anayamba kumufunafuna<br />
ndipo anamupeza pansi pa mtengo atafa. Atayang’ana<br />
mumtengo, anaona njoka ndipo anadziwa kuti ndi<br />
imene yamuluma. Makolowo ataona izi anati, “Mwana<br />
wathuyu wafa chifukwa cha mwano. Akanamvera<br />
zimene tinamuuza, sakanafa!”<br />
Phunziro: Mwana womvera amakhala ndi moyo<br />
wautali.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mwanayu anali ndi mavuto otani?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />
atafika kumunda anakwera mumtengo?<br />
3. Kodi anakumana ndi mavuto otani?<br />
4. Kodi akanatani kuti apewe mavuto amenewa?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
200
Bambo ndi Mwana Wake<br />
Tsiku lina bambo wina anakwera sitima limodzi ndi<br />
mwana wake. Sitimayo itangoyamba kuyenda,<br />
mwanayo anayamba kulongolola m’sitimayo ndipo<br />
amauza bambo ake kuti, “Ababa, taonani mitengo<br />
ikuthamanga! Taonaninso nyumbazi, zikuthamangatu<br />
ngati mphenzi!” Bambo akewo anangogwedezera mutu<br />
n’kumusiya. Anthu ena ataona izi anafunsa bamboyo<br />
kuti, “Kodi mwana wanuyu n’koyamba kukwera<br />
sitima?” Koma bamboyo anapukusa mutu. Kenako<br />
mwana uja anayamba kufuntha m’sitimayo, amati<br />
akaona chinthu, amachiyandikira kuti achionetsetse<br />
ndipo anthu ena anayamba kusowa naye mtendere.<br />
Ndiyeno munthu wina anauza bambo a mwanayo kuti,<br />
“Kodi mwana wanuyu mutu wake umagwira?<br />
N’chifukwa chiyani akungokhala ngati anadya matako<br />
a galu?” Ndiyeno bamboyo anayankha kuti, “Si bwino<br />
kupupuluma kuweruza munthu wina usakudziwa<br />
nkhani yonse. Pali mawu akuti, ‘osamaweruza<br />
munthu kuchokera pamene iweyo waima, koma<br />
kuchokera pamene munthuyo waima.’ Mawuwa<br />
amatanthauza kuti kumakhala kulakwa kumaweruza<br />
munthu pongotengera zimene ukuona. Pepani kuti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
201
mwana wangayu akukusowetsani mtendere, koma<br />
ineyo ndikumumvetsa. Mwanayutu anabadwa<br />
wosaona. Kuteroko panopa tikuchokera kuchipatala<br />
komwe anakamuchita opaleshoni ya maso moti<br />
wangoyamba kumene kuona. Chilichonse ndi<br />
chachilendo kwa iyeyu moti n’chifukwa chake<br />
akumangodabwa ndi chilichonse. N’chifukwa<br />
chakenso ineyo sindinamuletse. Ndimaona kuti<br />
akatopa asiya yekha.” Atamva zimenezi, anthuwo<br />
anamumvetsa moti anangogwira pakamwa.<br />
Phunziro: Osamafulumira kuweruza ena usakudziwa<br />
nkhani yonse.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi vuto la mwanayu linali chiyani?<br />
2. Kodi tinganene kuti mitengo yomwe ankaona<br />
inkathamangadi?<br />
3. N’chifukwa chiyani anthu ena anayamba<br />
kudabwa naye?<br />
4. Kodi pamene bamboyo anagwedezera mutu<br />
ankatanthauza chiyani? Nanga bwanji pamene<br />
anapukusa mutu?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
202
5. Kodi tinganene kuti anthu a m’sitima ija<br />
analakwitsa kuganiza kuti mutu wa mwanayo<br />
sugwira?<br />
6. Kodi mukuganiza kuti akanatani kuti adziwe<br />
vuto la mwanayo popanda kunena zachipongwe?<br />
7. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
203
Kupulumukira M’kamwa mwa Mbuzi<br />
Tsiku lina anyamata awiri anapeza mbuzi<br />
itamangidwa pamtengo wina ndipo anaganiza zoti<br />
aibe. Atangoyamba kumasula chingwe cha mbuziyo,<br />
mwini wake anabwera ndipo anawafunsa kuti,<br />
“N’chifukwa chiyani mukumasula mbuzi yanga?”<br />
Anthuwo anayamba kuchita mantha. Koma m’modzi<br />
anati, “Tinaona kuti pano palibe msipu wabwino,<br />
ndiye tinaganiza zoti tikaimangirire pamtengo uwo.<br />
Taonani msipu wake ukungoti biriwiribiriwiri,<br />
kukongola. Zoona mbuziyi ife ndi njala msipu uli<br />
m’khonde?” Mwini mbuziyo atamva zimenezi<br />
anawakhulupiriradi. Koma mbuziyo inkadziwa kuti<br />
anthuwo akunama. Ndiye chifukwa choti sitha<br />
kuyankhula, akubawo anapulumukira m’kamwa mwa<br />
mbuzi.<br />
Phunziro: Anthu ena amapulumuka chifukwa cha<br />
bodza.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
204
Mafunso<br />
1. Kodi cholinga cha anyamatawa chinali chiyani?<br />
2. Kodi ankanena zoona pamene ananena kuti<br />
amafuna kumangirira mbuziyo pamene panali<br />
msipu wabwino?<br />
3. Kodi anyamatawa anapulumukira pati?<br />
4. Tiyerekeze kuti munthu wina wapulumuka<br />
mwamwayi galimoto ikufuna kumugunda, kodi<br />
kungakhale kulondola titanena kuti wapulumukira<br />
m’kamwa mwa mbuzi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
205
Kodi Wochimwa Anali Ndani?<br />
Pa nthawi ina alimi 10 anali paulendo. Ali paulendowo<br />
kunayamba chimvula champhamvu komanso cha<br />
ziphaliwali. Alimiwo ataona kuti mvulayo ikhoza<br />
kuwapweteka, anaganiza zobisala m’kanyumba kena.<br />
Koma atafika m’kanyumbako, anaona kuti<br />
chiphaliwali china chinkangozungulira kanyumbako.<br />
Pamalopo panali chiphokoso choswa makutu, moti<br />
alimiwo anayamba kunjenjemera. Kenako anayamba<br />
kuganiza kuti n’kutheka zoti pakati pawo pali munthu<br />
wina wochimwa kwambiri, yemwe chiphaliwalicho<br />
chikufuna kuti chimuphe. Ndiye anaganiza zopeza<br />
munthuyo kuti amutulutse panja n’cholinga choti<br />
chiphaliwalicho chikamusasanthe. Anachita zimenezi<br />
chifukwa samafuna kuti chiphaliwalicho chiphetse<br />
anthu osalakwa. Alimowo anakambirana zoti akoleke<br />
zisoti zawo pamalo enaake ndipo munthu amene<br />
chisoti chake chitauluke ndi mphepo, ndi amene ali<br />
wochimwa. Atachita zimenezi, chisoti cha mlimi wina<br />
chinauluka ndipo alimi enawo atangoona zimenezi,<br />
anamugwira n’kumuponyera panja mopanda chifundo<br />
m’pang’ono pomwe. Koma munthuyo atangotuluka<br />
panja, chiphaliwalicho chinasiya kuzungulira<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
206
kanyumbako ndipo chinamenya denga la kanyumbako<br />
moopsa kwambiri moti alimi 9 anatsala aja anafera<br />
momwemo. Pamenepa m’pamene zinadziwika kuti,<br />
mlimi anamutulutsa uja ndi amene anali wabwino,<br />
ndipo chifukwa cha munthuyo chiphaliwalicho<br />
chinkangozungulira nyumbayo osaiomba. Ndiye<br />
pamene alimi 9 otsala aja anatulutsa mlimiyu,<br />
chiphaliwalicho chinaona kuti mpulumutsi wawo<br />
wachoka, ndipo chinalanga alimi oipa mtimawo mwa<br />
kuwapha. Chinawalanga chifukwa anatulutsa mnzawo<br />
paja, osamuchitira chifundo ngakhale pang’ono.<br />
Phunziro: Usanayambe kuloza kuipa kwa munthu<br />
wina, kumayamba kaye wayeza kuipa kwako.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
207
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani alimiwa anaganiza kuti<br />
pakati pawo pali munthu wina wochimwa amene<br />
chiphaliwalicho chinkamufuna?<br />
2. Kodi atamugwira n’kumuponyera panja<br />
chinachitika n’chiyani?<br />
3. Kodi tinganene kuti wochimwa anali ndani<br />
kwenikweni?<br />
4. Kodi mukunganiza kuti chikanachitika<br />
n’chiyani, akanamulola mlimiyu kukhalabe nawo<br />
limodzi?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
208
Mtsuko Wochucha Ndalama<br />
Kalekalelo kunali munthu wina wochakachika, yemwe<br />
anapeza mtsuko waukulu m’munda mwake. Kenako<br />
anayamba kuukumba ndipo atatero anautenga<br />
n’kupita nawo kunyumba kwake. Atafika anauza<br />
mkazi wake kuti autsuke. Koma mkazi wakeyo<br />
atangotsiramo sopo, mtsukowo unayamba kuchucha<br />
sopo wambirimbiri. Amati akakhuthula sopoyo, sopo<br />
winanso amatuluka n’kudzaza mtsukowo. Bamboyo<br />
anayamba kugulitsa sopoyo ndipo mtsukowo<br />
unapitirizabe kutuluka sopo wambiri moti bamboyo<br />
ankapeza ndalama zosaneneka. Koma tsiku lina,<br />
mwangozi, ndalama inagwera mumtsuko uja ndipo<br />
mtsukowo unasiya kuchucha sopo n’kuyamba<br />
kutuluka ndalama. Amati akazichotsamo, zina<br />
zimatulukanso, moti banjali linakhala ndi ndalama<br />
zankhaninkhani, n’kulemera. Ndiye munthuyo anali<br />
ndi bambo ake okalamba kwambiri, womwe ankakhala<br />
kumudzi wina. Bambo akewo analibiretu mphamvu<br />
zoti angadzisamalire, moti mwana wawoyo anawatenga<br />
n’kumakhala nawo. Koma atakhala kwa kanthawi,<br />
munthuyu anayamba kuona kuti bambo akewo ndi<br />
aulesi moti anawauza kuti azigwira ntchito yochotsa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
209
ndalama mumtsuko uja. Koma chifukwa cha<br />
ukalamba, bambowo zinkawavuta kuchita zimenezi<br />
ndipo mwana wawoyo anapsa mtima n’kuyamba<br />
kuwalalatira amvekere, “Ndinu munthu wamanja<br />
lende. N’chifukwa chiyani mukulephera kugwira<br />
ntchito yophwekayi? Pakhomo panotu timayendera<br />
mawu akuti wosagwira ntchito asadye. Ndiye ngati<br />
simukufuna kugwira ntchito, mudziwa chochita.”<br />
Zitatere gogoyo anakhumudwa kwambiri poona kuti<br />
mwana wake weniweni wayamba kumunyoza chifukwa<br />
choti ndi wopeza bwino. Kenako anangotembenuka ali<br />
pintchapintcha kuti atuluke panja. Koma atangotero,<br />
anapunthwa n’kugwera mumtsuko muja ndipo<br />
anafera momwemo. Nthawi yomweyo mtsuko uja<br />
unayamba kutulutsa mitembo yambirimbiri. Amati<br />
akachotsa ina, inkatulukanso ina. Ndalama zonse<br />
zomwe zinatuluka mumtsuko uja zinathera kuika<br />
maliro a bambo ake ndipo ankati akaika lero maliro,<br />
mawanso amakaika ena. Kenako munthuyo anafika<br />
potopa ndi kuika maliro a bambo akewo, moti anaswa<br />
mphikawo ndipo pamene ankauswa n’kuti ali<br />
kwakwatuke wotheratu, wosowa ndi ya mchere<br />
yomwe.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
210
Phunziro: Ukakhala pabwino, usamanyoze ena.<br />
Mafunso<br />
1. N’chiyani chinathandiza munthu wotchulidwa<br />
m’nkhaniyi kutuluka mu umphawi?<br />
2. Kodi anatani atazindikira kuti bambo ake<br />
sangakwanitse kudzisamalira okha?<br />
3. N’chifukwa chiyani anakwiya ataona kuti<br />
bambo akewo amalephera kuchotsa ndalama<br />
mumtsuko uja?<br />
4. Kodi mapeto ake anali otani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
211
Mphamvu Zobwereka<br />
Nthawi inayake, Nkhandwe inakumana ndi Kambuku.<br />
Kambukuyo atangomuona anatulutsa dzimano zake,<br />
n’kutulutsa zala zake n’kuyamba kuthamangira kunali<br />
Nkhandwe kuja kuti aidye. Koma Nkhandweyo inati,<br />
“Pepani achimwene, taimani kaye! Osamafulumira<br />
kuganiza kuti m’nkhalango muno amphamvu ndinu<br />
nokha. Mphamvu zanutu zikulenga, tikaziyerekeza ndi<br />
zanga. Tiyeni tiyendere limodzi, ndipo inuyo<br />
muziyenda pambuyo panga. Anthu akandiona ineyo<br />
koma osachita mantha, inuyo mundidye. Koma<br />
akandiona n’kuchita mantha, basi mundileke.”<br />
Kambukuyo anagwirizana ndi zimenezi ndipo<br />
Nkhandweyo inayamba kuyenda kulowera<br />
kwinakwake, Kambukuyo akutsatira pambuyo.<br />
Kenako anakumana ndi gulu la anthu ndipo ataona<br />
kuti kukubwera Nkhandwe, koma kumbuyo kwake<br />
kuli Kambuku, nthawi yomweyo analiyatsa liwiro la<br />
mtondo wadooka. Kenako Nkhandwe ija inati,<br />
“Waonatu, ndinali patsogolo ndine, koma anthu<br />
atandiona anachita mantha kwambiri moti<br />
anangotsala pang’ono kudziipitsira!” Kambukuyo<br />
ataona zimenezi anaona kuti mnzakeyodi ndi patali,<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
212
moti ananyamuka n’kuyamba kuthawa. Ankaganiza<br />
kuti anthu aja amathawadi Nkhandweyo, osadziwa<br />
kuti mphamvu zake zinali zochita kubwereka.<br />
Nkhandweyo inali itabwereka mphamvu za<br />
Kambukuyo, yemwe anthu aja anamuona akubwera<br />
pambuyo pake.<br />
Phunziro: Osamaopa mphamvu zochita kubwereka.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Nkhandwe inachita chiyani pofuna<br />
kudzipulumutsa?<br />
2. Kodi anthu aja ankathawa chiyani<br />
kwenikweni?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
213
Anzeru Omwe Anali ndi Vuto Losaona<br />
Kalelo kunali anthu ena asanu ndi awiri omwe anali<br />
ndi vuto losaona. Anthuwa anali anzeru kwambiri moti<br />
anthu ankawatayira katsatsa akamva zimene<br />
zinkatuluka pakamwa pawo. Ndiye tsiku lina anthuwa<br />
anaganiza zopita kumalo ena kuti akaone zinyama.<br />
Atafika kumeneko, anapita pamene panali njovu.<br />
Anthu anayi anagwira miyendo ya njovuyo, m’modzi<br />
anagwira chimulomo cha njovuyo, wina anagwira<br />
pamimba ndipo wina anagwira mchira. Ndiye yemwe<br />
anagwira chimulomo uja anayamba kuuza anzakewo<br />
kuti, “Ine ndiganiza kuti njovu imaoneka ngati njoka.”<br />
Koma mnzake amene anagwira kumchira uja<br />
anamutsutsa n’kunena kuti, “Iyayi, imaoneka ngati<br />
chingwe.” Ena amene anagwira miyendo aja<br />
anagwirizana chifukwa anati, “Nonsenu mukunama,<br />
njovu imaoneka ngati mtengo.” Koma amene anagwira<br />
pamimba uja anayamba kunena anzakewo kuti ndi<br />
wopanda nzeru ndipo anati, “Nonsenu ndi a ziwala<br />
m’maso, njovutu imaoneka ngati phiri.” Kenako anthu<br />
onsewo anayamba kukangana moti zinthu zinafika<br />
poipa kwambiri. Munthu wina yemwe ankangoonerera<br />
zimene zinkachitikazo anafika pamalowo ndipo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
214
anawauza kuti, “Aliyense wa inu wangogwira mbali<br />
imodzi ya njovuyi, moti mukanaphatikiza zomwe<br />
nonsenu mukudziwa, mukanatha kudziwa kuti njovu<br />
yonse imaoneka bwanji.”<br />
Phunziro: Palibe amadziwa zonse.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani anthuwa ankatsutsana?<br />
2. Kodi onsewo ankanama?<br />
3. Kodi akanatani kuti adziwe mmene njovu<br />
imaonekera?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
215
Nkhuku ndi Nkhunda<br />
Kunyumba kwina kunabwera alendo mwadzidzidzi.<br />
Ndiyeno paja kulandira alendo kumaonekera m’mbale,<br />
anthu a pakhomopo anaganiza zowaphikira nsima.<br />
Ndiye popeza anali ndi Nkhunda komanso Nkhuku,<br />
anayamba kukambirana kuti aphe chiyani. Ena ankati<br />
aphe Nkhuku pomwe ena ankati aphe Nkhunda.<br />
Nkhuku itamva zimenezi inayamba kukuwa kuti,<br />
“Koma nkhundayooooo!” Ndipo Nkhunda inkati,<br />
“Mulungu ngwamkulu, Mulungu ngwamkulu,<br />
Mulungu ngwamkulu!” Nkhuku ija inkasokosa<br />
kwambiri moti anthu aja anaiona. Ndiyeno wina anati,<br />
“Bwanji tiphe Nkhuku, chifukwa tikapha Nkhunda,<br />
tipha zambiri.” Nkhukuyo inapitirizabe kukuwa kuti,<br />
“Koma nkhundayooooo!” Ndiye basitu, anthu aja<br />
anayamba kuthamangitsa Nkhuku ija ndipo ataigwira<br />
anaipha, moti maliro ake, alendo aja anadyera nsima.<br />
Phunziro: Osamakankhira anzako mavuto, chifukwa<br />
zimatha kutembenuka.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
216
Mafunso<br />
1. Kodi zimene Nkhuku ndi zimene Nkhunda<br />
imanena m’nkhaniyi kutabwera alendo zikufanana<br />
ndi mmene zenizeni zimalirira?<br />
2. N’chifukwa chiyani eni khomo anaganiza zopha<br />
Nkhuku?<br />
3. Kodi Nkhuku inakankhira bwanji makala<br />
pamalaya a mnzake?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
217
Mankhwala a Banja<br />
M’mudzi wina munali mayi wina, yemwe nthawi zonse<br />
ankangokhalira kudandaula kuti banja lake<br />
silikuyenda bwino. Ankasirira kwambiri akaona<br />
anzake amene anakwatira ndi kumbuyo komwe,<br />
akusangalala ndi mabanja awo. Banja lake linali ndi<br />
vuto limodzi. Mwamuna wake ankangokhalira<br />
kumukutumula ndipo iye ankaona kuti amayesetsa<br />
kumusamalira komanso kuchita zonse zofunika.<br />
Ankati akapita kwa alangizi, ankangomuuza kuti,<br />
“Banjatu n’kupirira, ndiye kaya mwamuna wanu<br />
akumakukunthani, muzingopirira basi. Banja ndiye<br />
limenelo!” Ndiye atatopa ndi nkhanza zimene<br />
mwamuna wake ankamuchitira, anaganiza zopita kwa<br />
munthu wina wodziwa zitsamba kuti akamupatse<br />
mankhwala achikondi. Atafika kwa munthuyo,<br />
anamufotokezera zonse ndipo munthuyo<br />
sanachedwechedwe koma kulowa m’tchire<br />
n’kukathyola kamtengo kenakake. Anamupatsa<br />
mayiyo n’kumuuza kuti, “Mukakakangofika<br />
kunyumba kwanu, musakayankhule chilichonse.<br />
Mukangoika kamtengo aka m’kamwa mwanu<br />
n’kukhala chete. Musakayerekeze kutsegula<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
218
pakamwa, chifukwa mukakatero, mankhwalawa<br />
akasuluka.” Mayiyo anauyambadi wakwawo ndipo<br />
atafika anatsatira malangizo anapatsidwa aja.<br />
Mwamuna wake atabwera, anamuphikira nsima<br />
n’kukamupatsa, ndipo mwamunayo anati,<br />
“Ndinakuuza kuti ndili ndi njala?” Mkaziyo atamva<br />
mawu osayamikawo anapsa mtima kwambiri, koma<br />
chifukwa choti anauzidwa kuti asatsegule pakamwa,<br />
sanayankhe chilichonse. Mwamuna uja anadabwa<br />
kwambiri ndi zimenezi, moti anangotenga nsimayo<br />
n’kuyamba kudya. Kungoyambira tsiku limenelo<br />
mwamuna wakeyo sanamumenyenso ndipo patapita<br />
masiku angapo, mayiyo anapitanso kwa munthu<br />
wazitsamba uja kuti akamuthokoze, ndipo<br />
anamufotokozera kuti mankhwala anamupatsa aja<br />
akuthandizadi. Koma munthuyo anati, “Sikuti ndi<br />
mankhwalawo amene akukuthandizani. Ndi mtengo<br />
wachabechabe womwe ndinathyola m’thengomo. Vuto<br />
lanu mayi ndi kulongolola! Mpofunika muphunzire<br />
kuweta lilime lanulo.”<br />
Phunziro: Mavuto ambiri amene timakumana nawo<br />
amayamba chifukwa cha pakamwa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
219
Mafunso<br />
1. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani banja la<br />
mayiyu silinkayenda bwino?<br />
2. Kodi vuto la mayiyu linali chiyani?<br />
3. Kodi mankhwala amene munthu wodziwa<br />
zitsamba uja anamupatsa ndi amene anathandiza<br />
kuti banja lake liziyenda bwino?<br />
4. N’chifukwa chiyani tiyenera kusamala ndi<br />
pakamwa pathu?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
220
“Ndifera Manyazi Mkazi Wanga”<br />
Tsiku lina Aphiri anauza akazi awo kuti, “Mkazi<br />
wanga, zinthu ndiye zativuta. Tipange bwanji kuti<br />
tipeze ufa? Sindingalole kuti ana angawa afe ndi njala<br />
ine ndikuona. Koma ndisanameyi, palibe chimene<br />
ndikuona kuti ndingachite.” Kenako anapukusa mutu<br />
wopanda nyanga. Mkazi wakeyo anavomerezadi<br />
zimene mwamuna wake ananena ndipo<br />
anawalimbikitsa kuti asadandaule. Kenako<br />
mwamunayo anati, “Mkazi wanga, ndaganiza pulani.<br />
Bwanji ineyo ndinyengezere kumwalira? Ndiye uike<br />
mbale pamsewupo. Anthu akamaponya ndalama<br />
zachipepeso, iweyo uzipita kukazichotsamo<br />
n’kukazibisa.” Koma mkaziyo anafunsa mwamuna<br />
wakeyo kuti, “Nanga bwanji anthu akayamba kubwera<br />
pakhomo pano? Kodi ndiwauza chiyani akanena kuti<br />
akupititseni kumotchale? Mukafa ndi kuziziratu inu?”<br />
Bamboyo anati, “Usadandaule ndi zimenezo, ineyo<br />
ndichita zinthu zoti asazindikire kuti ndili moyo. Koma<br />
akanena kuti andipititse kumotchale, iweyo ukane.<br />
Ungowonetsetsa kuti ndalama zomwe zikuponyedwa<br />
m’mbale zikuyenda bwanji. Ineyo ndidzuka mawa<br />
anthu asanaganize zotulutsa maliro panja.”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
221
Mkaziyo anagwirizana ndi maganizowo ndipo<br />
mwamunayo ananamiziradi kumwalira ndipo mkazi<br />
wakeyo anayamba kulira. Mbale inaikidwadi pamsewu<br />
ndipo anthu anayamba kuponyamo. Posakhalitsa<br />
anthu ena anayamba kuyenda m’midzi n’kumatolera<br />
ufa, nkhuni komanso ndalama ndipo akabwera nazo<br />
ankazipereka kwa mayi uja. Ndiyeno m’mawa kutacha,<br />
anthu anayamba kubwera ndipo ena anakagula<br />
bokosi n’kunyamula Aphiri n’kuwaikamo. Koma<br />
atawaika m’bokosimo, Aphiri tulo tidawatenga.<br />
Mkazi uja ankayembekezera kuti mwamuna wake<br />
adzuka. Koma ataona kuti sakudzuka, anapita pafupi<br />
ndi bokosilo n’kuyamba kulira amvekere, “Inu bambo<br />
a Pofera tadzukani chondeeee! Tadzukani inuuu!<br />
Ndimayesa munati mudzuka inu!” Azimayi anabwera<br />
kudzatonthoza mnzawoyo poganiza kuti chisoni<br />
chamugwira. Pamene bamboyo ankadzuka n’kuti<br />
pakhomopo pali namtindi wa anthu ndipo Aphiri<br />
atamva phokoso la anthuwo komanso nyimbo<br />
zachisoni zikuimbidwa, anachita manyazi kuti adzuke.<br />
Mkazi wawo uja anapitirizabe kulira mouza mwamuna<br />
wakeyo kuti adzuke, koma Aphiri anangoti zii. Amati<br />
akamva mkazi wawoyo akulira ankangonena<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
222
chapansipansi kuti, “Ndifera manyazi mkazi wanga!”<br />
Posakhalitsa kunabwera adzukulu kuchokera<br />
kumanda ndipo anatenga misomali n’kuyamba<br />
kukhoma bokosilo. Amati akati khoo! Mayi uja amalira<br />
mosatonthozeka, “Amunanga inu dzukani, chonde<br />
tadzukani. Nditani nawo ine anawa?” Kenako<br />
anakhomanso wina kuti khoo mpaka anamaliza.<br />
Anthu ankangoganiza kuti mayiyo akuyankhula<br />
zimenezo chifukwa cha chisoni, osadziwa kuti<br />
akunena nkhaninkhani. Pamapeto pake anthu<br />
ananyamula bokosi lija ndipo Aphiri anakaikidwa<br />
m’manda chifukwa cha manyazi.<br />
Phunziro: Osalola kulowa m’mavuto chifukwa cha<br />
manyazi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
223
Mafunso<br />
1. Kodi Aphiri ataona kuti zinthu zavuta<br />
panyumba pawo anapanga pulani yotani?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti anawerengera mtengo<br />
wake?<br />
3. N’chifukwa chiyani Aphiri ankachita manyazi<br />
kudzuka?<br />
4. N’chifukwa chiyani anthu sanadabwe ndi<br />
mawu amene akazi a Aphiri ankanena akamalira?<br />
5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
224
Atambwali Sametana<br />
M’mudzi wina munali atsinzina n’tole awiri. Wina<br />
dzina lake linali Paguza ndipo wina anali Saguza.<br />
Tsiku lina Paguza anatenga thumba la mpunga<br />
n’kuikamo mchenga ndipo pamwamba pa mchengawo<br />
anaikapo mpunga n’cholinga choti thumbalo lizikhala<br />
ngati lodzadza mpunga okhaokha. Nayenso Saguza<br />
anatenga mtsuko n’kuthiramo madzi ndipo<br />
pamwamba pamadziwo anathirapo mafuta. Madziwo<br />
ankangoti ndengundengu ngati mafuta ndipo<br />
anasenza mtsukowo n’kumapita nawo kumsika.<br />
Atafika kumeneko, atambwaliwa anakumana ndipo<br />
anagwirizana kuti angosinthana zinthuzo. Paguza<br />
anauza mnzakeyo kuti, “Uwu ndi mpunga<br />
wopunthapuntha, wabwino kwambiri moti<br />
simungapezenso wina yemwe angakugulitseni mpunga<br />
ngati umenewu. Mukakauphika uzikangotuluka<br />
umodziumodzi.” Saguza atamva zimenezo anaona kuti<br />
wapeza munthu watulo, moti sanachedwe koma<br />
kuvomera zoti asinthane ndi mnzakeyo mtsuko<br />
wamafuta. Aliyense anangosenza katundu anapatayo<br />
n’kuuyamba wakwawo. Koma atafika kunyumba<br />
anazindikira kuti apusitsana. Paguza ataona kuti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
225
mnzakeyo wamugulitsa madzi anayamba<br />
kumusakasaka ndipo atamupeza anamufunsa kuti,<br />
“N’chifukwa chiyani wandipusitsa?” Mnzakeyonso<br />
anamufunsa kuti, “Nanga n’chifukwa chiyani iwe<br />
wandigulitsa mchenga?” Atazindikira kuti zawo<br />
n’zimodzi, anayamba kugwirizana kwambiri. Tsiku lina<br />
anapangana kuti apite kukaba kwa mfumu<br />
yam’mudzimo. Atambwaliwa anamva zoti mwana wa<br />
mfumuyo, yemwe anali kutheba, wabwera ndi<br />
chikwama chodzadza ndalama ndipo wapatsa bambo<br />
ake. Atamva zimenezi mitima yawo inkangoti<br />
dyokodyoko, ndipo anagwirizana kuti akumane pakati<br />
pa usiku n’cholinga choti akasowetse chikwamacho.<br />
Kenako anauyamba wa kunyumba kwa mfumuyo.<br />
Mwamwayi pakhomo la mfumuyi panalibe zifuyo<br />
zaukali, moti Paguza anakwanitsa kulowa m’nyumba<br />
ya mfumuyo aliyense osadziwa. Kenako anayenda<br />
monyang’ama n’kukanyamula chikwama chachikulu<br />
chomwe chinali kumutu kwa mfumu yomwe inali<br />
tapatapa ndi tulo. Ndiyeno anafika nacho pazenera la<br />
nyumbayo n’kupatsira Saguza, yemwe anaima panja<br />
pa nyumbayo. Saguza atangolandira chikwamacho<br />
anayamba kuthawa nacho. Atafika kunyumba kwawo,<br />
anasonkhanitsa mudzi wonse ndipo anauza anthu a<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
226
pakwawopo kuti ali ndi chikwama chodzadza<br />
ndalama. Koma anawauzanso kuti, “Pali vuto limodzi.<br />
Munthu winawake akundilondalonda. Akufuna<br />
atatenga chikwamachi.” Anapitiriza kunena kuti,<br />
“Ndalamazi zikhoza kupangitsa kuti aliyense pamudzi<br />
pano akhale mponda makwacha. Ndiye mulola kuti<br />
munthu ameneyu atenge ndalamazi?” Anthuwo<br />
atamva zimenezi anapukusa mitu yawo n’kunena kuti,<br />
“Ayi.” Ndiyeno Saguza anati, “Ndikufuna kuti tibise<br />
chikwamachi, Paguza akabwera, mudzamuuze kuti<br />
ndamwalira.” Anthuwo anagwirizana nazo zimenezo<br />
ndipo posakhalitsa anthu anayamba kubuma<br />
amvekere, “Mayi wawaye, tilowera kuti ife, achimwene<br />
athu atsogolaa.” Pakhomopo panayamba kumveka<br />
chiphokoso chachikulu ndipo posapita nthawi<br />
panyumbapo panadzaza anthu. Ndiyeno m’mawa<br />
kutacha, Paguza anatulukira ndipo anafunsa anthu a<br />
pakhomopo kuti, “Wamwalira ndi ndani?” Anthuwo<br />
anamuyankha kuti, “Mnzanu ujatu anatipeza<br />
m’bandakucha ndipo amanena kuti sakumva bwino<br />
moti anatikomokera m’manja, basitu ulendo unali<br />
womwewo.” Koma Paguza atamva zimenezi anayamba<br />
kukayikira ndipo anati, “Anthuwa akundiuza kuti<br />
Saguza wamwalira. Amwalira bwanji atathawa ndi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
227
chikwama chandalama. Akufuna kundiyenda pansi<br />
ameneyu!” Kenako anauza anthu a pakhomopo kuti,<br />
“Ndingakaone mtembo wake?” Anthuwo anamutengadi<br />
n’kumulowetsa m’chipinda chimene munali<br />
mtembowo. Kenako anayamba kuyankhula ndi<br />
mnzakeyo kuti, “Bwanawe, dzuka kuti tingokambirana<br />
bwinobwino?” Koma mnzakeyo anangoti zii. Kenako<br />
Paguza anauza azimayi ena kuti, “Nditerekereni madzi,<br />
awire ngati ososolera nkhuku.” Azimayiwo anachitadi<br />
zimenezo, mosadziwa kuti akufuna achite nawo<br />
chiyani. Madziwo atabwadamuka, azimayiwo<br />
anawatenga n’kupita nawo kwa Paguza. Paguza<br />
analandira madziwo n’kupempha kapu yake<br />
yotungira. Ndiyeno anayamba kuuza mtembowo kuti,<br />
“Ambwana, dzuka zinthu zisanafike poipa! Koma<br />
mnzakeyo sanayankhe. Kenako anatunga madzi<br />
otentha aja pang’ono, n’kumutsira pamwendo kuti<br />
chwaa! Koma mnzakeyo anapirira ndipo sanatekeseke.<br />
Kenako anatunganso ena n’kumuthiranso kuti chwaa!<br />
koma ayi ndithu Saguza sanasunthe. Ndiyeno Paguza<br />
anati, “Bwanawe, dzuka. Uvulalatu!” Koma Saguza<br />
sanayankhe. Kenako Paguza anati, “Nanga mtembo<br />
umamva kuotcha ngati? Kuti nditsimikizire kuti<br />
mnzangayu wapitadi, ndingomukhuthulira madzi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
228
onsewa.” Ndiyeno anangotenga mtsuko uja<br />
n’kukhuthulira mnzakeyo ndipo Saguza analephera<br />
kupirira. Anadzambatuka kwinaku akulira ndipo<br />
mnzakeyo anati, “Ndinakuuzatu ine, ukanangodzuka<br />
nthawi yomwe ija sukanavutika chonchi.” Pa nthawiyi<br />
n’kuti Saguza atayamba kukupuka m’miyendo ndi<br />
m’mikonomu. Zitatero Paguza ndi Saguza<br />
anagwirizana kuti agawane ndalamazo mofanana,<br />
ndipo anakatenga chikwama chija kuti ayambe<br />
kugawana. Koma atangochitsegula, anapeza kuti<br />
munali mapepala okhaokha.<br />
Phunziro: Utambwali umabweretsa mavuto.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi Paguza ndi Saguza anali anthu otani?<br />
2. N’chifukwa chiyani anayamba kugwirizana?<br />
3. N’chiyani chikusonyeza kuti onsewa anali<br />
adyera?<br />
4. Kodi pali chilichonse chimene anapindula?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
229
Mutu Wodwala Kansire Adatema Kadzidzi<br />
Kalekale pakati pa mbalame zonse, panali kambalame<br />
kena kakang’ono kotchedwa Kansire, enanso amati<br />
Tchala. Kambalameka kankalemekezedwa ndi<br />
mbalame zonse chifukwa mbalamezo zinkati Kansire<br />
ndi mbalame ya ku mizimu, kapena kuti mbalame<br />
yomvana ndi mizimu.<br />
Kansire amati zipatso ndi zakudya zina zikasowa, iye<br />
amaulukira kumanda kotchedwa Makololo n’kuyamba<br />
kulira. Posapita nthawi m’mitengo yonse kumandako<br />
zipatso zimvekere kuti mbwee! kholophethee! Nthambi<br />
za mitengoyo kuti petaa! kulemedwa ndi zipatso<br />
zikuluzikulu.<br />
Tsopano zimati zikatero, phokoso la mbalame<br />
limachita kuti, buu! Panali mbalame ina imene<br />
inkamveka kwambiri ndi phokoso. Mbalameyi inali<br />
yotchedwa Pumbwa. Pokondwerera zipatso zija<br />
mumtengo wa Kachere inkati, “Mbwe, mbwe, bzolo,<br />
bzolo, zanchulukira! zanchulukira!” Tsopano<br />
mbalamezo zikakhuta, zimatera pansi n’kuyamba<br />
kuyamika mbalame ija yotchedwa Kansire.<br />
Kuyamikako inkatsogolera ndi mbalame ija yomveka<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
230
kwambiriyi, Pumbwa. Mbalameyo imati “bzoli! bzoli!<br />
zanchulukira! Ife tiyamika inu Kansire. Lero ife<br />
laponda lamphawi diwa. Tinali padzuwa koma inu<br />
Kansire mwatitoletsa nkhwangwa ndi mpini womwe.<br />
Popanda inu Mfumu Kansire, ife sitikanasambira<br />
m’nkhali monga tachitiramu. Mwa ichi tiyamika,<br />
taphuka chifukwa cha inu mfumu yathu Kansire,”<br />
Anatero Pumbwa poyamika Kansire. “Mawa tibwera<br />
ndi mitolo ya nsembe kuti mupereke kwa mizimu ya<br />
makolo athu,” anatero poyamikira Kansire.<br />
Pumbwa anapitiriza motere, “Pano tikufuna<br />
kukutsimikizirani kuti ndinu mfumu yathu. Enawa<br />
timangowaona chimwendo kong’akong’a, kutalika<br />
chikhosi apoo, kusololokera m’mwamba, koma palibe<br />
chimene adatichitirapo, koma kumangotigogomola ndi<br />
kutinzonzomola pamitu!”<br />
Nthawi yomweyo panamveka mawu ozaza, “Iwe<br />
Pumbwa! thula! Bwanji ukuchitira chipongwe ine?<br />
Kodi kutalika mwendoko ndidakumanani ndine?”<br />
Anatero Nthiwatiwa ali kupalasika ndi ukali, masaya<br />
atatupikana ndi mkwiyo. Mbalame zonse zinangoti<br />
maso pa Nthiwatiwa, yuuu! n’kumangoinyodogola cha<br />
mumtima zili “Ho! Tamuonani gudu wogudukira<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
231
zinthu za eni ake. Tachionani chimwendo kutalika<br />
ngati mitengo ya m’masano.” Mmene zimateromo<br />
zimatunguluza maso, lilime lili pamtunda, milomo<br />
zitapambanitsa kupitiriza kunyodola a Nthiwatiwa aja.<br />
“Ine ndikunenetsa pano!” a Nthiwatiwa anatero,<br />
“Mbalame zonse ndinu opusa kwambiri. Mudzaleka liti<br />
kugodomala kotere? Simungatchule kamwana aka ka<br />
Kansire kuti ndi mfumu. Kodi simukudziwa kuti<br />
mfumu ndine Nthiwatiwa? Kodi n’chilungamo<br />
kumalemekeza Kansire, muleka ife amuna ogona<br />
kukhomo kosatseka? Kodi simudziwa kuti Kansire ndi<br />
nthumbidwa? Kodi Kansire ndi ine titati tipandane<br />
angafe ndani?” Anatero Nthiwatiwa poonetsa kunyada.<br />
“Ndiponi mutalemekezako a Mphungu awo, kaya a<br />
Ng’ongwe awo, a Namng’omba kaya a Namntchichi<br />
awo, kapenanso a Kadzidzi awo chifukwa chokula<br />
mutuwo . . . ”<br />
“Ine ndikuthilira ndemanga mawu amenewo!” anatero<br />
a Namn’gomba, “Mbalame nonsenu muli ndi kaduka<br />
kachinangwa! Si zaulemu kumalemekeza kafinye aka<br />
ka Kansire kamene ife timakatchula kuti kandakhuta<br />
kale ayi!” a Namng’omba anatero powonjezera<br />
ndemanga.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
232
“Zoonadi,” anatero Ng’ongwe ali kutsokomola,<br />
chithokomiro cha pakhosi chili tugwaa! kutupikana<br />
ndi ukali. “Ine ndili kuvomereza Namng’omba.<br />
Kamwana aka ka Kansire sikangakhale mfumu a<br />
Nthiwatiwa ali pompano ayi. Kodi ufumuwo alandirira<br />
chifukwa cha ulosi wokhawokhawo? Kodi chidadza ndi<br />
yani choti munthu akakhala wa kumizimu, wotiitanira<br />
mvula tsono, n’kumatinso yemweyo akhale mfumu?”<br />
anatero Ng’ongwe pofunsa mbalame zonse zija.<br />
Mmenemo n’kuti atawatunguluzira maso ali pamtunda<br />
ngati maso a njoka ija yotchedwa mamba, pam’mero<br />
pali dyokhodyokho chifukwa cha ukali. Mbalame<br />
zonse zija zinangotinso maso pa Ng’ongwe kuti yuu!<br />
“Mwaona nokha palibe woyankha, kutsimikiza kuti<br />
sindikunena zambwerera ayi!” anatero Ng’ongwe.<br />
Nthawi yomweyo Ng’ongwe anapisa mutu wake<br />
mphiko lakumanzere. Potulutsa mutu wake, mbalame<br />
zonse zija zinadodoma poona kuti kukamwa kwake<br />
kunali ndudu ya fodya ili fuubaa! utsi umenewo. Utsi<br />
wina unali kutulukira mphuno.<br />
“Kansire ntchito yake ndi ulosi basi osatinso za ufumu<br />
zizimvekera pa dzina lakenso, izo takana<br />
kwamtuwagalu.” Anatero Ng’ongwe ndudu ija<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
233
atayamba waitula pansi, koma utsi wina ukutulukabe<br />
m’mphuno pamene anali kuyankhula.<br />
“Kambalame kena ngati Pumbwa, kasasokoneze<br />
Kansire ayi. Mulekeni iye azingolingalira njira zabwino<br />
zomvanirana nazo ndi mizimu ya makolo athu amene<br />
adafa kale basi. Amfumu anthu a Nthiwatiwa ndiwo<br />
amene azilinganiza za ufumu wawo monga<br />
zokonzekera za kumeta unamwali pa nthawi<br />
ikubwerayi ya zinamwali za anyamata ndi<br />
asungwana,” anatero Ng’ongwe popumulira<br />
kuyankhula kuja. Ng’ongwe anatolanso ndudu ija ya<br />
fodya, ndiye tsopano kudangooneka kuti, toloooo! Utsi<br />
umenewo mapiko ake ali kuwombetsa m’mimba<br />
kuonetsa ukali, m’menemo n’kuti maso ali psuu! ngati<br />
wopemereredwa ndi utsi kudzenje.<br />
“Chimene tiyenera kumakumbukira n’choti<br />
tisamaiwale sing’anga wathu Mleme kumuitana kuti<br />
nayenso adzadye nawo phwandoli. Taonani ife<br />
zithokomiro zili tugwaa! chimkhuto chimenecho.<br />
Nanga bwanji taiwala ng’anga yathu? Amfumu<br />
Nthiwatiwa akankhe mthenga kwa Mleme kuti abwere<br />
adzadye nawo ufulu talandirawu . . . azimu atigwera<br />
m’mbale . . . atigwera m’mitengo yathuyi kumasano<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
234
kuno,” anateronso Ng’ongwe fodya ali fubafuba utsi uli<br />
kutulukira m’mphuno.<br />
“Wayankhula bwino iwe Ng’ongwe!” anatero<br />
Nthiwatiwa. “Nonsenu musamvere zija amanena<br />
Pumbwa zija ayi. Zija ndi zoyankhula akapasule<br />
okhaokha. Pumbwa sadziwa kuti dziko ndi mafuwa<br />
achita kuchilikiza. Zoyankhula za Pumbwa ndi<br />
zochotsa mafuwa kuti dziko ligwe. Motero, zimene<br />
wayankhula Pumbwa zija aliyense angozithira<br />
kunkhongo. Woyamwa yekhayekha ndi amene<br />
amayankhula zokhuta ngati zimene zija,” Nthiwatiwa<br />
anateronso ali kupenyetsa Pumbwa uja. “Motero tonse<br />
tiyenera kumwazikana koma tonse tidzakumanenso<br />
pano m’mawa dzuwa likutuluka kuti tidzapitirize<br />
kudya madyelerowa.”<br />
M’mawa kutacha dzuwa likutuluka, mbalame zonse<br />
zinali zitasonkhana kale kumasano kuja koma zonse<br />
zinali zitatera pansi zili kwangopenyetsetsa zipatso<br />
m’mitengo muja. Zinali kudikira ulamuliro wa<br />
mbalame ija ya kumizimu yotchedwa Kansire. “Nanga<br />
Kansire ndi Chiuzimbi ali kuti?” Anafunsa motero a<br />
Nthiwatiwa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
235
“Ife sitikudziwa mfumu,” anatero Kadzidzi chimutu<br />
chake chachikulu chija chili nguninguni kugwedezeka,<br />
masaya ali kweevee! ngati wodwala matenda a<br />
kadukutu. “Tonse tabwera, mphachi (kupatula) awiri<br />
mwatamulawo,” anawonjezera motero Kadzidzi.<br />
Dzidzidzi, mbalame zonse zinamva kukwapulitsa kwa<br />
mapiko a mbalame kuti phururu! phururu!<br />
Posakhalitsa zinaona Chiuzimbi akutulukira ali kutera<br />
pansi, Chiuzimbi chachitali ngati chimchira cha<br />
Nkhwere chili vwandaa! Chilinunda ngati cha kunzi ya<br />
ng’ombe chili pholi! pamsana. “Suyo Chiuzimbi uja<br />
mfumu!” anatero Kadzidzi.<br />
“Eya, ndamuona,” Nthiwatiwa anatero.<br />
“Pepani mfumu ndachedwa kufika!” Anatero<br />
Chiuzimbi.”<br />
“Chifukwa?” Nthiwatiwa anafunsa, maso ali psuu!<br />
mutu uli njenjenje ndi ukali.<br />
“Pepani mfumu ndiye kuti . . . ” anangoyamba motero<br />
Chiuzimbi. “Ndiye kuti chiyani? Kodi iwe Chiuzimbi<br />
umanyadira chimthenga chako chachitalichi? Kapena<br />
umanyadira linundali basi n’kumadziyeseza kuti<br />
ndiwe ng’ombe eti? Ife sitingadikire iwe pano<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
236
kutichedwetsa phwando lathuli limene adatipatsa<br />
mlosi wathu Kansire. Kansire pomvana ndi mizimu ya<br />
makolo athu taona m’mitengomu zimene Chisumphi,<br />
kaya Chauta, kaya Mphambe anatipatsa. Kodi<br />
umadziyesa ng’ombe iwe eti?” Anatero Nthiwatiwa<br />
podula pakamwa Chiuzimbi.<br />
“Zachisoni mfumu Kansire wafa?” anatero Chiuzimbi<br />
kuti zonena zake zimveke msanga.<br />
“Ukuti chiyani? Kansire wafa?” Nthiwatiwa anafunsa.<br />
Nthawi yomweyonso panamveka kubuma maliro a<br />
Kansire. Dothi lonse pamalo onsewo linali madzi<br />
khathikhathi ndi misozi yochokera m’maso a mbalame<br />
zija. Nthiwatiwa sanathenso kuyankhula chifukwa cha<br />
phokoso lachisokonezo motere: “Bzolobzolo, bzoii,<br />
mbwembweembwe, gulululu, khurururu, fwakafwaka,<br />
kweeefu, mbirombiro!”<br />
“Nena bwino, ukuti chiyani za Kansire?” Nthiwatiwa<br />
anafunsanso.<br />
“Kansire zoonadi,” anatero Chiuzimbi, “wadwala<br />
pafupi imfa.”<br />
“Khalani chete,” Nthiwatiwa anatero. Chifukwa cha<br />
mawu wotsirizira aja a Chiuzimbi, panali bata kungoti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
237
ziii. “Ndikuti Kansire wadwala pafupi imfa. Usiku<br />
anakomoka katatu.”<br />
“Chabwino, iwe wemwe Chiuzimbi pita kwa sing’anga<br />
wathu Mleme ku Chinsiro ukamuuze za matendawo.<br />
Nonse mubwere pamodzi kuti tonsefe tipitire limodzi<br />
kwa Kansire. Wamva bwino?” anatero Nthiwatiwa.<br />
“Zikomo mfumu,” anatero Chiuzimbi akuuluka kupita<br />
kwa ng’anga ija.<br />
“Zikomooo,” anatero Chiuzimbi.<br />
“Eyaa,” anatero Mleme.<br />
“Koma musavutike n’kundikonzera pokhala ayi.<br />
Ndikhala pachikuni ndatera pano,” Chiuzimbi anatero.<br />
“Kodi n’kwabwino?” Mleme anafunsa.<br />
“Ayi si kwabwino.”<br />
“Chavuta n’chiyani?”<br />
“Matenda kwathuku.”<br />
“Wadwala ndani?”<br />
“A Kumizimu a Kansire.”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
238
“Tsono zikatero n’cho chiyani, atilosere zinthu ndani?”<br />
“Ndimo taonera. Mutu ndithu udawayamba dzana.<br />
Ngakhale amayenda kungoti munthu uja ngolimba.<br />
Mwinanso kuchepa thupi kuwombola. Usiku<br />
anakomoka katatu. Amfumu a Nthiwatiwa atamva ndi<br />
amene anandikankhira nkhongo kunowa, ali basi<br />
muzikabwerera limodzi.”<br />
“Zikomo ndamva. Ine bwenzi n’tabwera ndithu popeza<br />
madzulo ndinalandira mthenga woti kuli phwando,<br />
wosadziwanso kuti n’kumamva zoteronso. Chabwino<br />
dikira pomwepo nditenge lumo lakuthwa loti<br />
tikatemere mankhwala kuti mnzathuyo achire<br />
msanga. Komatu zina leku zina kambu, ine dzinali<br />
ndimangolimva koma titakumana m’malunje, ayi<br />
ndithu sindingawadziwe, mpang’ono pomwe.”<br />
“Aaa! zoonadi?”<br />
“Zoonadi pali agogo kumanda.”<br />
“Tiyeni mukawadziwa lero.”<br />
“Ndakondwanso podzandiitana ine. Koma dzuwa<br />
lisanalowe, Kansireyo akhala atachira.”<br />
“Zoonadi zimenezi?”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
239
“Eee, ine ndimanena zoona zokhazokha. Palibe<br />
ng’anga yoopsa ngati ine m’dziko lonse lino. Ndili ndi<br />
mankhwala anga owopsa kwambiri.”<br />
“Mudakatenga kuti mankhwalawo?”<br />
“Kwathu kudziko la mbewa.”<br />
“Kodi inu ndimayesa kuti kwanu ndi kwathu kudziko<br />
la mbalame. Kodi inu sindinu m’bale wathu?”<br />
“Ndine m’bale wanu.”<br />
“Nanga bwanji mukuti kwanu ndi kwa mbewa?”<br />
“Inenso ndikufunseni. Kodi inu kwanu n’kuti?”<br />
“Ndakuuzani kale kuti kwathu ndi kwa mbalame.”<br />
“Osati kwa ng’ombe?”<br />
“Chifukwa?”<br />
“Nanga inu mwadabwa ndi chiyani poti muziti ndikati<br />
kwathu ndi kwa mbewa mudodoma. Inenso ndili<br />
kudodoma poti mukuti kwanu n’kwa mbalame pomwe<br />
ine ndikuona kuti kwanu n’kwa ng’ombe.”<br />
“Chifukwa chiyani?”<br />
“Achimwene ndikuuzeni. Inu kwanu n’kuwiri: kwa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
240
ng’ombe ndiponso kwa mbalame.”<br />
“Mwaneneranji zimenezi?”<br />
“Taonani chilinundacho! Ine kwathu n’kwa mbewa ndi<br />
mbalame. Tonsefe ndife ofanana tilibe kwathu<br />
kwenikweni ayi. Izi tinazivala mosasankha ayi,<br />
tinangopezeka monga tililimu ndiponso . . . ”<br />
“Pepani sing’anga tiyeni tingakapeze maliro.”<br />
Dzidzidzi, mbaleme zonse ku makololo kuja<br />
zidangoona a Chiuzimbi ndi a Mleme ali kutera pansi<br />
koma maso a Mleme anali pa Kadzidzi gaa, chifukwa<br />
adaona kuti mutu wake unali wotupa. Mleme<br />
mumtima mwake anaganiza kuti mbalame ija<br />
yotchedwa Kansire ndi Kadzidzi uja, poona<br />
kutupikana kwa mutu.<br />
Nthawi yomweyo anatulutsa lumo lakuthwa kwambiri<br />
pamodzi ndi mankhwala ake. Posakhalitsa mbalame<br />
zonse zinaona kuti mutu wa Kadzidzi watemedwa kale<br />
magazi ali psuu, mankhwala ali kupakidwa.<br />
“Pepani sing’anga, ine sindikudwala ayi,” anatero<br />
Kadzidzi.<br />
“Kodi wodwala mutuyo sindiwe?” anafunsa Mleme.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
241
“Ayi sindine.”<br />
“Nanga ndi ndani?”<br />
“Kansire.”<br />
“Ali kuti?”<br />
“Kuchisa chake.”<br />
“Nanga iwe sukudwala?”<br />
“Ayi.”<br />
“Nanga mutuwu unatupa n’chiyani?”<br />
“Siwotupa, ndi mmene ndinabadwira basi, monga<br />
momwe mulili inumu. Mumaoneka ngati mnzathu<br />
mbalame, komanso ena amati ndinu mbewa. Kodi<br />
zikatero chikhale chifukwa choti ife tikutemereni<br />
mankhwala kuti umbewa muli nawowu ukuchokeni?”<br />
“Aaaa, . . . chipongwe choopsa, ndizo<br />
m’mandiyitanira?” anatero Mleme ali kuuluka<br />
kuthawira m’malunje, mbalame zonse zili maso yuu,<br />
kumupenya koma chimutu cha a Kadzidzi chili magazi<br />
psuu.<br />
Phunziro: Si bwino kumaweruza anthu pongotengera<br />
maonekedwe chifukwa maonekedwe amapusitsa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
242
Mafunso<br />
1. Kodi ndi mbalame iti imene inali yotchuka ndi<br />
phokoso?<br />
2. N’chifukwa chiyani mbalameyi inkaona kuti<br />
ndi bwino kuti Kansire akhale mfumu?<br />
3. Mukuganiza kuti n’chiyani chinachititsa kuti<br />
Chiuzimbi abwere mochedwa?<br />
4. Kodi Kansire sanapite kuphwando lija<br />
chifukwa chiyani?<br />
5. N’chiyani chinachititsa Mleme kuganiza kuti<br />
amadwala mutu ndi Kadzidzi?<br />
6. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
243
Chikumbumtima Chidapha Njovu<br />
Kalekalelo, Njovu inkacheza kwambiri ndi Kalulu.<br />
Tsiku lina inapita kwa Kalulu, n’kumupeza kulibe,<br />
koma inapeza panja patayanikidwa ndiwo. Itaona kuti<br />
palibe aliyense akuona, inaganiza zongoziba. Kenako<br />
Njovu inatenga ndiwozo n’kumapita nazo kwawo.<br />
Kalulu atafika n’kupeza ndiwo zake zitabedwa,<br />
anaganiza zokafunsa bwenzi lake la pamtima Njovu.<br />
Kalulu anafunsa a Njovu kuti, “A Njovu, kodi<br />
mwatenga ndiwo zanga ndinu?” A Njovu anakana kwa<br />
m’tu wagalu, amvekere, “Ndatenga si ine!” Kenako<br />
Kalulu anati, “Koma ngati mwatenga ndinuyo<br />
n’kumakana, chikumbumtima chikuphani!” Kenako<br />
Kalulu anaona msana wa njira. Njovu m’mbuyo muno<br />
inayamba kuda nkhawa kwambiri. Inkaganiza kuti<br />
chikumbumtima ndi nyama yaikulu komanso<br />
yamphamvu kwambiri kuposa iyoyo, choncho<br />
inayamba kukhala mwamantha. Inasiya kutuluka<br />
panja kukafuna chakudya poopa kukumana ndi<br />
chikumbumtima. Masiku anadutsa Njovu ikungogona<br />
nayo njala moti inaonda kwambiri. M’kupita kwa<br />
nthawi Njovu inafa. Apa mawu a Kalulu aja anathera<br />
mu siizi, Njovu inaphedwa ndi chikumbumtima.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
244
Phunziro: Ukachita chinthu choipa chikumbumtima,<br />
chomwe ndi munthu wamkati, chimakuimba mlandu<br />
moti utapanda kuvomereza kulakwa kwako ukhoza<br />
kufa ndi nkhawa.<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi chikumbumtima ndi chiyani?<br />
2. Kodi Njovu inkachidziwa chikumbumtima?<br />
3. Kodi n’chiyani chinapha Njovu?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
245
Chifukwa Chake Chule Amakhala M’madzi<br />
Pamudzi wina panali mayi ena odziwa kulikazinga<br />
thobwa. Dzina la mayiwa linali Zenje. Anzawo ena<br />
achilomwe ankangowatchula kuti mayi Nalimata.<br />
Anthu ambiri ankabwekera thobwa la mayiwa moti<br />
anthu sankatha phazi pakhomo pawo. Mwamwayi,<br />
mayi Zenje anali munthu wochereza alendo.<br />
Ankalandira aliyense amene wabwera kudzacheza<br />
ndipo ankamupatsa chipanda cha thobwa kuti<br />
azizilitse kukhosi. Sankasamala ngakhale zitakhala<br />
kuti munthuyo ndi kabwerebwere. Koma panali<br />
munthu wina wopanda pabwino, yemwe ngakhale<br />
mayiwa ankamuchitira zabwino zonsezi,<br />
ankawaberanso thobwa lawo. Munthu ameneyu dzina<br />
lake linali Chule. Ankati mayi Zenje akangochoka<br />
kupita kuchitsime kapena kumsika, iyeyo<br />
ankawalowela m’nyumba n’kuwabera thobwa. Mayi<br />
Zenje akabwera ankadabwa kuti thobwa lawo latsika.<br />
Kenako anazindikira kuti pali tambwali wina yemwe<br />
akumapungula thobwalo ndipo anatsimikiza mtima<br />
zomukhaulitsa. Kuyambira tsiku limenelo<br />
anachenjera, moti anayamba kukhoma chitseko<br />
chawo. Chulenso naye anazindikira kuti amutulukira<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
246
ndipo anapeza njira ina yobera thobwalo ngakhale<br />
zitakhala kuti pakhomo ndi pokhoma. Mayi Zenje<br />
ataona kuti kukhoma chitseko sikukuthandiza,<br />
anaganiza zowiritsa kwambiri thobwalo kuti wakubayo<br />
akabwera limuwaule. Ndiyeno anawiritsa thobwa<br />
lomwe anaphika tsikulo n’kuliika pakona la nyumba<br />
yawo. Kenako anadendekera mtsuko wawo n’kumapita<br />
kumadzi. Chule ataona kuti mphaka wachoka, anaona<br />
kuti yakwana nthawi yoti khoswe asangalale. Popeza<br />
pakhomo la nyumba ya mayi Zenje panali potseka,<br />
anapita kuseri kwa nyumbayo n’kukwera pamtondo.<br />
Kenako anasolola bango lake n’kulilowetsa mumtsuko<br />
unali pakona uja kudzera pazenera. Kenako<br />
anayamba kupopa thobwalo ndi mlomo wake. Monga<br />
mwa masiku onse, iye ankayembekezera kumva<br />
kuzuna kwa thobwalo. Koma patsikuli anakumana<br />
nazo. Thobwa lothenthalo linamulowa kukhosi moti<br />
anabuula koopsa. Thobwalo linawauliratu kukhosi<br />
kwake ndipo mawu ake anasinthiratu. Kenako<br />
analumphira pansi ndipo thobwa lija linapitirizabe<br />
kutuluka m’bango lija moti linayamba<br />
kumupungukira pamsana. Msana wonse unatuluka<br />
matuza ndipo nthawi yomweyo anathamangira<br />
kumadzi kuti akadziziziritse. Kungoyambira nthawi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
247
imeneyo, Chule anayamba kukhala m’madzi kuti<br />
asamamve kupweteka kwambiri chifukwa cha matuza<br />
anali pansana pake aja.<br />
Phunziro: Kuba ndi koipa. Kuba ndi kutenga chinthu<br />
cha mwiniwake popanda chilolezo.<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi mayi Zenje anali munthu wotani?<br />
2. Kodi anatani atazindikira kuti thobwa lawo<br />
likubedwa?<br />
3. Kodi Chule anasiya kuba thobwa ataona kuti<br />
mayi Zenje akumatseka chitseko chawo?<br />
4. Kodi mayi Zenje anatani pofuna kukhaulitsa<br />
amene ankawabera thobwa lawo?<br />
5. N’chifukwa chiyani mawu a chule anasiya<br />
kumveka bwino?<br />
6. N’chifukwa chiyani Chule amakhala ndi zilonda<br />
pamsana?<br />
7. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
248
Kufulumira Kunena Anathawitsa Likongwe<br />
wa Apongozi<br />
Panali anyamata awiri amene anakwatira banja<br />
limodzi. Wina anakwatira wamkulu wina anakwatira<br />
wamng’ono. Tsiku lina apongozi awo anadwa la<br />
matenda odetsa nkhawa. Atapita kwa sing’anga<br />
anawauza kuti mankhawala amene angathandize kuti<br />
apongoziwo achile ndi mbewa ya Likongwe. Akamwini<br />
awiri aja atamva zimenezi ndiponso pokhala odziwa<br />
kusaka ndi kukumba mbewa, analonjeza kuti apeza<br />
Likongwe amene anali kufunikayo. Tsiku lotsatira<br />
mkamwini wamkulu uja anauza mkamwini<br />
wamng’ono pamodzi ndi anzawo amene amachita<br />
nawo chidyerano kuti apite kokapha Likongwe<br />
chifukwa anali ataona pamene pamalowa Likongwe.<br />
Asanayambe kukumba, mkamwini wamkulu uja anati,<br />
“Amene athawitse Likongwe wa apongoziyu akachoka<br />
pamudzi paja.” Mkamwini wamng’ono pofuna<br />
kusonyeza ulemu kwa mkamwini wamkulu anayamba<br />
kukumba. Pasanapite nthawi, Likongwe anadziwa kuti<br />
zinthu zavuta, kenako anabulika kudzenje lija<br />
n’kulinjika mbali imene kunakhala mkamwini<br />
wamkulu uja. Mkamwini uja chifukwa chamantha<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
249
anajowa, osadziwa kuti akupereka mpata woti<br />
Likongwe athawe. Likongwe analowa patchire<br />
osaonekanso. Mankhwala othandizira apongozi<br />
sanapezeke. Tsopano ena anafunsa kuti, “Wathawitsa<br />
Likongwe ndani?” Mkamwini wamkulu anayesetsa<br />
kupepesa koma chifukwa anali atanena kale yekha<br />
kuti amene athawitse Likongweyo achoka pamudzipo,<br />
anakakamizika kuchoka ndi mkazi wake. Mkamwini<br />
wamng’ono ndi amene anapitiriza kukhala pamudzipo.<br />
Phunziro: Osamafulumira kuyankhula chifukwa<br />
umatha kudziika wekha pakona.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani akamwiniwa ankakumba<br />
Likongwe?<br />
2. Kodi mkamwini wamkulu ananena kuti amene<br />
athawitse Likongwe achita chiyani?<br />
3. Kodi zimene ananenazi zinamubweretsera<br />
mavuto otani?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
250
Mlendo Ndi Mame<br />
Kalekale panali mayi wina dzina lake Nasiketi. Nasiketi<br />
anali kudziwika kwambiri chifukwa cha umbombo.<br />
Tsiku lina anavuula mphale, ndipo atasinja ufa<br />
anaganiza kuti ndiwo zimene adyere nsima tsikulo<br />
zikhale nyama. Anasinjadi ufa wosalala bwino<br />
ndiponso anapezadi nyama yonona bwino imene<br />
anakagula pamudzi woyandikana ndi mudzi wawo. Pa<br />
nthawiyi Nasiketi anali asanataye matsukwa a mphale<br />
ija. Akumaliza kuphika nsima anamva panja munthu<br />
wina akuodira. Poonetsetsa anaona kuti ndi mlendo<br />
amene sanali kumuyembekezera. Apa nzeru<br />
zinamuthera Nasiketi. Ananyamula nsima ndi kuika<br />
pamphika wa nyama uja kenako n’kuika mphika wa<br />
nyama ndi nsima ija pakamwa pa mtsuko umene<br />
munali matsukwa uja. Tsoka ndi ilo nyama ndi nsima<br />
ija zinagwera m’matsukwa muja. Atatuluka panja kuti<br />
akumane ndi mlendo uja, mlendoyo anamuuza kuti,<br />
“Pepani ndi wosakhalitsa, ndimafuna mundigawireko<br />
madzi akumwa.” Mlendoyo atamwa madziwo<br />
ananyamuka n’kumapita.<br />
Phunziro: Umbombo kapena dyera zimawonongetsa<br />
zambiri.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
251
Mafunso<br />
1. Kodi Nasiketi anali ndi khalidwe lotani?<br />
2. Kodi ataona kuti kwabwera alendo anachita<br />
zotani kuti alendowo asadye nawo nsima yake ya<br />
ndiwo nyama?<br />
3. Kodi alendowo anabwera kunyumba kwake<br />
chifukwa chiyani?<br />
4. Kodi mukuganiza kuti Nasiketi anasangalala<br />
ndi nsima ija?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
252
Ukasauka Usamagwira Nyanga<br />
Mkulu wina anakafunsira ntchito kwa bwana<br />
wolemera kwambiri. Kumene ankagwira ntchitoko<br />
anapezako anzake amene anali atakhala kwa nthawi<br />
yaitali ndi bwanayo. Anzakewo anali ndi zinthu<br />
zambiri zimene anapata pa zaka zimene anakhala<br />
akugwira ntchito. Chifukwa chosirira kukhala ndi<br />
katundu ngati wa anzakeyo ndiponso kukhala<br />
wolemera, anaganiza zoti apeze mankhwala. Mumtima<br />
anaganiza kuti mankhwalawo amuthandiza kuti<br />
bwana wake azimukonda, kuti iye akhupuke ndiponso<br />
kuti bwanayo achotse ena mwa anzake ena amene<br />
sankagwirizana nawo. Ngati zimenezi zikanatheka<br />
ndiye kuti iye akanalandira udindo ndiponso<br />
akanamuwonjera malipiro ake. Atapita kwa sing’anga<br />
anapezadi mankhwala amene ankafunawo. Sing’anga<br />
uja popereka mankhwalawo anamuuzitsa kuti<br />
asakagone kwa masiku atatu chifukwa ngati<br />
angakagone ndiye kuti akatupa mimba. Koma tulo ndi<br />
nkhondo timagoneka olira. Tsiku loyamba analimbadi<br />
m’maso osagona. Pamene kunkacha tsiku lachiwiri<br />
tulo tinali titasonkhana, moti amati akati aimirire<br />
sizimatheka. Atakhala pansi kuyambika kwa matenda<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
253
kunali komweko. Anzake amene ankafuna kuwalodza<br />
aja atamufunsa anafokotokoza kuti, “Pepani anzanga,<br />
munthune ndimafuna kulemera. Ndiye mankhwala<br />
amene ndinapeza, chizimba chake china n’choti<br />
ndisagone masiku atatu, koma ndalephera<br />
kuchikwaniritsa. Motero thamangani mukamuuze<br />
sing’anga wandipatsa mankhwalawa kuti atsukule<br />
nyangayo n’cholinga choti ine ndikhale ndi moyo.”<br />
Anzake aja atapita anakapeza kuti sing’anga uja anali<br />
atamwalira cha dzana lake moti anthu anali<br />
asanachoke pasiwa. Anzake atabwerako<br />
anamufotokozera mmene ayendera. Chifukwa<br />
chodziwa kuti kwake kwatha anayamba kulira ndipo<br />
polirapo anali kulira mochenjeza kuti, “Abale anga<br />
munthu ukasauka si nzeru kugwira nyanga, taonani<br />
zandichitikira inezi!” Pamenepo anzakewo<br />
anavomerezadi kuti, “Ukasauka usamagwire nyanga.”<br />
Nyanga zimene munthu uja anakatenga ndi zimene<br />
zinam’phetsa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
254
Phunziro: Anthu ambiri a ku Africa kuno<br />
amakhulupirira zanyanga kapena ufiti, koma ngati<br />
atasukusula akhoza kuona kuti ufiti kulibe. Mwambi<br />
wakuti ukasauka usamagwira nyanga<br />
umangochenjeza kuti zikativuta tisamachite zinthu<br />
zomwe zingatiike m’mavuto kapena kumafunira<br />
anzathu zoipa.<br />
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani mkuluyu anapita kwa<br />
asing’anga?<br />
2. Kodi kusakhutira ndi zomwe tili nazo<br />
kungabweretse mavuto anji?<br />
3. Kodi mwambi wakuti ukasauka usamagwira<br />
nyanga umatanthauza chiyani?<br />
4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
255
Ulenje Umasimba Wako<br />
Kalekale panali munthu wina amene anapita kuthengo<br />
kukapha nyama. Kumeneko anapha nyama ziwiri.<br />
Pamene ankabwerera kwawo n’kuti kunja kuli<br />
kachisisira ndipo anamva phokoso likumveka m’mudzi<br />
wakwawo. Atafika pamphambano, mwadzidzidzi<br />
anangoona mkango watulukira. Mlenjeyo anachita<br />
mantha kwambiri, koma mkango uja unamuuza kuti,<br />
“Musachite mantha achimwene. Panotu takumana<br />
amuna okhaokha. Kaya inu mukuchokera kuti<br />
ulendowu?” Poyankha munthu uja anati: “Ine<br />
ndikuchokera m’malunjemu ndimakasaka.” Ndiyeno<br />
mkango unati, “Popeza tonse tikuchokera kosaka,<br />
aliyense asaulule mnzake. Ulenje umasimba wako,<br />
osati wamnzako.” Atangosiyana pamenepo, mkango<br />
uja unalowa m’tchire ndipo munthuyo anathamangira<br />
kwawo ali ndi mantha. Kenako anayamba kuuza<br />
anthu kuti wakumana ndi mkango utagwira nyama.<br />
Mkango uja utamva zimenezi, unapita kunyumba kwa<br />
amfumu n’kukagwira mwana wawo n’kumupha.<br />
Kenako unakamuika m’nyumba mwa mlenje uja.<br />
M’mudzimo munayambika chipwirikiti chifukwa cha<br />
kusowa kwa mwanayo ndipo mfumu inalamula kuti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
256
anthu afufuze amene watenga mwana wakeyo.<br />
Atafufuza anapeza mwanayo atafa koma ali m’nyumba<br />
mwa mlenje uja ndipo mfumu inalamula kuti nayenso<br />
aphedwe.<br />
Phunziro: Si bwino kumaulula zinthu zomwe iwenso<br />
wachita nawo, zimabweretsa mavuto.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi mkango unkachokera kuti nanga mlenje<br />
uja ankachokera kuti?<br />
2. N’chifukwa chiyani mkango unanena kuti<br />
ulenje umasimba wako?<br />
3. Kodi mlenjeyo analakwitsa chiyani?<br />
4. Nanga anakumana ndi mavuto otani?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
257
Angozo ndi Mwana Wawo<br />
Bambo: Iwe Joni, kodi pulezidenti woyamba m’Malawi<br />
muno anali ndani?<br />
Mwana: Joyce Banda.<br />
Bambo: (Phwaaa! anamuswa khofi) Uzikhala siliyasi<br />
ndi maphunziro ako!<br />
Mwana: Oo! pepani, ndimaona ngati mumafunsa<br />
pulezidenti woyamba wachizimayi.<br />
Bambo: Khala chete chimwana chopanda nzeru iwee!<br />
Ngati zikukuvutani zakupulaimale, ndiye<br />
zakusekondale mukaphula kanthu inu?<br />
Mwana: Chabwino, nanga inu bambo, Abengo ndi<br />
ndani?<br />
Bambo: Mlimi wa fodya.<br />
Mwana: (Phwaaa! naye analipulumutsa lake khofi)<br />
Abengo ndi chibwenzi cha amayi! Muzikhala siliyasi<br />
ndi banja lanu inu!<br />
Bambo: Mwanawe ndiuze zambiri.<br />
Mwana: Khalani chete. Ngati mukulephera kudziwa za<br />
akazanu musanakalambe, nanga mukadzakalamba<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
258
ndiye zidzakhala bwanji?<br />
Phunziro: Aliyense amachita bwino mbali inayake.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi n’chifukwa chiyani Angozo anamenya<br />
mwana wawo?<br />
2. Kodi makambitsirano a bambo ndi mwanayu<br />
akusonyeza bwanji kuti onse anali ndi nzeru?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
259
Ufulu wa Nkhwere<br />
Tsiku lina Nkhwere zinachoka m’nkhalango n’kufika<br />
pakhonde la sukulu yotchedwa Nfunde. Mtsogoleri wa<br />
Nkhwere anali Goloti. Goloti anasuzumira pawindo<br />
n’kuona mnyamata wina dzina lake Sibo akusewera<br />
m’kalasi ndipo anamuuza kuti: “Iwe Sibo, ife timafuna<br />
kuimba nawo sukulu, kodi aphunzitsi ako ali kuti?”<br />
Sibo anati, “Ine ndinatsiriza kale, tsopano ndine<br />
mphunzitsi.” Koma Goloti anati, “Kodi sudziwa kuti<br />
iwe ndi ife ndi mtundu umodzi? Inuyo munachokera<br />
kwa ife, mumangoona kunyada inuyo. Inu anzathu<br />
mumavala malaya ndi kabudula, ife timangokhala<br />
osavala, kodi mulibe manyazi kumanyoza ife makolo<br />
anu? Pakanapanda ife mukanaoneka inu?” Koma Sibo<br />
anati, “Sindikukudziwani ayi! Inu ndi anyani a<br />
m’tchire!” Koma Goloti anati, “Eee! Mwana uyu<br />
n’ngosaphunzira. Kawerengenso mabuku ako. Ife<br />
tsopano tikufuna ufulu womaimba sukulu pamodzi<br />
ndi inu, ndiponso tizichita zibwenzi ngakhalenso<br />
kukwatirana.”<br />
Sibo: “Chokani anyani inu!”<br />
Goloti: “Eee! Mwana iwe ukuchitira chipongwe makolo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
260
ako, ndithu mukapitiriza kuchita mwano umenewu<br />
mvula simuiona chaka chino.”<br />
Sibo: “Chokani inu! Chokani!”<br />
Goloti: “Ine ndi wapampando wa anzangawa.<br />
Tapangana m’tchire m’dalaka njoka. Ife tonse tikufuna<br />
tibwerere kumudzi kuno, tizidyera pamodzi, ndiponso<br />
tizimwera pamodzi.”<br />
Sibo: “Pakati pa ife ndi inu ayi, chibwenzi<br />
sichingakhalepo. Inu adakusankhirani Fulu kuti<br />
muchite naye ubwenzi.”<br />
Goloti: “Chabwino, tsala bwino, ife tipita kwa Fuluyo.<br />
Koma kawerengenso mabuku. Iwe unachokera mwa<br />
ife. Onani kamwana kosaphunzira, kawerenge<br />
mabuku a Dalawini, akakuuza. Onani umbuli! Funsa<br />
aphunzitsi ako!”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
261
Mafunso:<br />
1. N’chifukwa chiyani nkhwere zinkanena kuti ndi<br />
pachibale ndi Sibo?<br />
2. Kodi munthu ndi nyani ndi zofananadi?<br />
3. Kodi mukuganiza kuti nkhwere italowa<br />
m’kalasi n’kukhala padesiki ingaphunzire<br />
kalikonse?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
262
Ubwenzi wa Nkhumba ndi Nkhosa<br />
Kalekalelo, pakati pa Nkhosa ndi Nkhumba panali<br />
chibwenzi chonyambitana mapazi. Kumene Nkhosa<br />
inkayenda, Nkhumba inkakhala komweko. Anthu onse<br />
ankasilira chibwenzi chosaonekaoneka chotere. Kalulu<br />
nthawi zonse amati akamva za chikondi chotere<br />
sankamva bwino, kumtima kwake kunali nsanje.<br />
Tsiku lina Kalulu ankakambirana ndi mkazi wake<br />
amvekere, “Kodi iwe wamva za chikondi cha Nkhosa<br />
ndi Nkhumba?” Poyankha mkazi wake anati, “Eee!<br />
Anzanutu amenewo. Si zainuzi. M’nyumba<br />
kumangokangana tsiku ndi tsiku. Ndiponso pakhomo<br />
panga pano, ndimangokhalira kulandira milandu.<br />
Kumene mumayendako ntchito ndi bodza komanso<br />
kuchenjeretsa anthu. Mbiri ili buuu! Akuti<br />
kuchenjera! Banja lanunso likukukanikani kusamala!”<br />
Kalulu atamva mawu amenewa anati, “Izo udamvazo<br />
ndi za nsanje. Anthu amachita nsanje ndi ine popeza<br />
ife a Kalulu ndife amuna osati masewera. Mfumu<br />
yamuno m’nkhalango yomveka ngati kulira kwa<br />
mphenzi nthawi ya mvula.”<br />
Tsopano kalulu analowedwa mzimu woyipa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
263
Ananyamuka nalo liwiro kupita kwa Nkhumba ndipo<br />
anangoti balamanthu! nati, “Moni a Nkhumba! He-e-e!<br />
ati ndili ndi bwenzi! Mwamva kodi?” Kenako a<br />
nkhumba anati, “Zotani? Za bwenzi zotani?” Kalulu<br />
anati, “Suja akuti bwenzi lanu ndi a Nkhosa? Ine<br />
ndathamanga kudzaulula zimene anandiuza.” “Ine<br />
sindifuna kumva chilichonse chokhudza bwenzi langa<br />
Nkhosa, bwenzi lapamtima,” anatero a Nkhumba.<br />
Kenako Kalulu anati, “A Nkhosa amakunenani ati inu<br />
ndinu auve wodya zotoleza m’matope, ati ndinu<br />
msambamatope.”<br />
Tsopano nkhumba inautsa mutu wake kuti imve<br />
zonse.<br />
Kalulu: “Tere amatinso inu ndinu wamatekenya.”<br />
Nkhumba: “Tsopano ndakhulupirira, iwe Kalulu ndiwe<br />
wabwino. Iweyo ukhala bwenzi langa. Uzindiuza zonse<br />
zimene Nkhosa izinena.”<br />
Kalulu: “Chabwino ndavomera chibwenzi chapakati pa<br />
inu ndi ine.”<br />
Nkhumba: “Tsopano pita bwino bwenzi langa. Koma<br />
wosakamuuza Nkhosa kuti ndapanga ulendo<br />
wokamuphwasura iyeyo.”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
264
Kalulu analiyatsa liwiro lopita kwa Nkhosa. Atayipeza<br />
Nkhosa anati:<br />
Kalulu: “O! o! Kodi mulipo? Akadakhala kuti amafa<br />
ndi mjedo, kunena zoona n’kadakupezani mutafa.”<br />
Nkhosa: “Kwagwa chiyani?”<br />
Kalulu: “Ee ho! Ine panjira ndinakumana ndi a<br />
Nkhumba, zimene amanena zosonyeza kuti zija<br />
timamva kuti mumakondana, n’zabodza.”<br />
Nkhosa: “Amati chiyani iyeyo?”<br />
Kalulu: “Amati inu ndinu wanyansi ati sadzadyera<br />
nanu pamodzi popeza muli ndi matenda a mamina<br />
wosatha, amangochucha ngati mtsinje. Msipu wonse<br />
ati inu mudagwetsera mamina mudawononga.”<br />
Nkhosa: “Amatero iyeyo?”<br />
Kalulu: “Iwowo ndithu ndiwo amatero.”<br />
Nkhosa: “Kuyambira lero chibwenzi chachipongwe<br />
chotere chatha. Tsopano iweyo ndiwe bwenzi langa<br />
chifukwa umanena zoona, ndipo ndili pa ulendo<br />
kupita kwa iyeyo kuti ndikamuphulitse.”<br />
Pamene nkhumba inatsiriza kukwera chitunda<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
265
chopitira kwa Nkhosa inangoti, gululu yakumana ndi<br />
Nkhumba. Eee, panalitu moto!<br />
Nkhumba: “Bwanji iwe umandinena, lero kuli<br />
ndikupha!”<br />
Nkhosa: “Iwenso umandinena, ndamva kwa kalulu<br />
bwenzi langa. Lero ndikufinya.”<br />
Kupandana kwa awiriwa kunamveka ponseponse<br />
ndipo chibwenzi chinatha. Kalulu anati kwa mkazi<br />
wake: “Suja unkanena kuti chikondi chikundikanika,<br />
n’kumayamikira a Nkhumba ndi a Nkhosa, wamva<br />
tsopano zimene zachitikazi? Heede!<br />
Ndimangokumvetserani!”<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi mkazi wa Kalulu ankadandaula chiyani?<br />
2. Kodi khalidwe la Kalulu linali lotani?<br />
3. N’chifukwa chiyani Nkhosa ndi Nkhumba<br />
zinapandana?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
266
Mvundula Madzi<br />
Kalekalelo panali midzi iwiri imene anthu ankamvana.<br />
Anthu ambiri anali kusirira machitidwe a midziyi.<br />
Mayina a midzi anali Mchirawagaru, mwachidule<br />
amati mudzi wa Mchira. Winawo unali mudzi wa a<br />
Zeze.<br />
Pakati pa mudzi wa Mchira ndi wa Zeze, panali<br />
chitsime chotchedwa Namtudza. Chitsimechi chinali<br />
chokumba ndipo chinazunguliridwa ndi mitengo ya<br />
nkhadze cha kumtunda kwake. Kumunsi kwake<br />
kunali mtengo wamango ndipo chakumwera kwake<br />
kunali mtsinje umene udagwera ku Mtema, ku<br />
Phukuto m’mudzi mwa a Mchira modzera kumalo<br />
wotchedwa Danani, mpaka m’chikonde pafupi ndi<br />
Nzama kukaphera mumtsinje wa Namachizi. Kunsi<br />
kwake kunali dziwe lotchedwa Kanyinda.<br />
Chimbalame chotchedwa Mvundulamadzi,<br />
mwachidule amati Vundula chinali kumwera pa<br />
chitsime cha Namtuza, chimwera ku Mtema,<br />
Chimwera pa Chimkonde, mpaka dziwe la Kanyinda.<br />
Mbalameyi inali kuuluka pamwamba pa midzi iwiriyi,<br />
Mchira ndi Zeze, ndipo chifukwa cha kumvana kwa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
267
midzi iwiriyi Vundula sankakondwera ayi. Popeza<br />
Mbalame zotere zimakondwera zikaona chidani,<br />
maliro, ndewu kapena kuzokozana.<br />
Tsiku lina chinagona mumtengo wamkuyu pa<br />
Kanyinda. Mmawa chinalawira kuchitsime cha<br />
Namtunda ndipo chinaona gulu la akazi lasenza<br />
mitsuko kukatunga madzi. Gululi linali la kwa<br />
Mchirawagalu. Atatha kutunga, chimbalamechi<br />
chinalowa pachitsime paja basi n’kudetseratu madzi<br />
aja chimvekere, vu! vu! vu! Ndi mapiko ake aja, phi<br />
phi! phi! Madzi onse kuderatu kuti bii!<br />
Chitatero chingangoti vuuku, bisalu mumtengo wa<br />
Nkhadze. Tsopano akazi a kwa Zeze analipo khumi.<br />
Atafika pachitsime anapeza madzi ali bii! Mtsikana<br />
wina wotchedwa Maleyi anati, “Oo anzathu onani<br />
madzi ada! Komatu akazi a kwa Mchirawagaru atunga<br />
pompano. Basi iwowo ndi amene adetsa madzi.<br />
Akufuna kuti chitsime chikhale chawo chokha.<br />
Tsopano tadziwa, a Mfumu a Mchira akudana ndi a<br />
Zeze, awatuma ndi amfumu kuti adzachite zimenezi!”<br />
Akazi onse anabwerera osatunga madzi mpaka ena<br />
anapita kukatunga kuchitsime cha Namachizi.<br />
Chimbalame chija chitaona zimenezi chinangoti,<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
268
“Ehede! Basi zakhala bwino. Tsopano cholinga changa<br />
chakwaniritsidwa.”<br />
Tsiku lina m’mawa chimbalame chija chinasokoloka<br />
m’nthochi za m’madimba a ku Dumbzi, kulawirira ku<br />
Namtunda kukadetsanso madzi akazi a kwa a Zeze<br />
atatunga kale. Pobwera a kwa Mchira anapeza madzi<br />
akuda. Mtsikana wina dzina lake Damalesi anati,<br />
“Onani akazi a kwa Zeze adetsa madzi, awapangira ndi<br />
amfumu awo.” Onse anabwerera ndipo Mbalame ija<br />
pakumva inati, “Eheee, zanga zikuyenda bwino.”<br />
Potsiriza, midzi yonse inadodoma popeza mfumu<br />
ziwirizi zinafunsana pabwalo. Tsopano a Zeze ndi a<br />
Mchira anapangana kukakhalira ku chitsime kuja ndi<br />
nduna zawo. Mmawa kukucha, anaona chimbalame<br />
chabwera m’madzi muja lowu, chimvekere mapiko<br />
tambasulu, chayamba kuvu! kuvu! kuvu!<br />
Onse aja anathamanga ndi uta, basi n’kuchilasa ndipo<br />
chinafera pomwepo. Zitamveka izi, a Zeze ndi a<br />
Mchirawagaru pamodzi ndi anthu awo, anayanjananso<br />
chifukwa anapha mvundula madzi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
269
Phunziro: Ifenso tiziyamba tapha mvundulamadzi<br />
tisanayambe kudana.<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi mbalame yotchedwa Vundula<br />
inkasangalala pakachitika zotani?<br />
2. N’chifukwa chiyani midzi ya a Mchira ndi a<br />
Zeze inadana.<br />
3. Kodi anatani kuti adziwe amene ankadetsa<br />
madzi?<br />
4. Nanga ifeyo tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
270
Chifukwa Chake Ng’ona Imakhala M’madzi<br />
Kalekale dzikoli likali nsoka, panali mfumu ina<br />
yomveka kwambiri m’dziko lotchedwa Peta. Dzina la<br />
Mfumuyi linali Chifuyo.<br />
Dziko la Peta lidali loopsa. Kudali nkhalango ndipo<br />
m’nkhalangoyo mudali zilombo zosiyanasiyana zoopsa,<br />
kuyambira zokwawa mpaka zoyenda. Zimamveka kuti<br />
kunali njoka zowuluka ngati mbalame zomwe<br />
zinkatchedwa Njokambala. Zimamvekanso kuti kunali<br />
mikango yamapiko imene inkatchedwa Mkangombala.<br />
Mfumu chifuyo inali yolimba mtima pogonjetsa<br />
zilombo zonse m’dziko la Peta. Tsiku lina, mfumuyi<br />
inaitanitsa zamoyo zonse zam’tchire. Zitasonkhana<br />
padambo, Mfumu Chifuyo inati, “Ndakondwa kuti a<br />
Njovu, a Mkango, a Njati, a Nyamalikiti kaya a<br />
Kadyansonga, a Mvuwu komanso a Kalulu afika.”<br />
Nthawi imeneyi nyama zonse zinkangopenyetsana<br />
kwinaku zikumangonong’ona. Njovu inati, “Anzathu,<br />
inu a Mkango tasenderani kuno, uzaninso a Njati<br />
akhale pafupi. Kodi a Mvuwu, munthu ameneyu<br />
atisunga muno? Onani chili m’dzanja mwakecho. Kodi<br />
sichija amatiphera nachochi?” Kodi mphamvu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
271
imeneyi, adakayitenga kuti?” A Mkango anati, “Tiyeni<br />
tileke kuyankhula, angaganize kuti tamugalukira.”<br />
Mfumu Chifuyo inati, “Tsiku lina nyama ina inabwera<br />
kudzafunsa mmene ndizikusungirani, ndiye lero<br />
ndaganiza zoti ndiyankhe nkhani imeneyi. Ndikufuna<br />
kukhazikitsa malamulo oti aliyense aziyendera.<br />
Malamulo ake ndi awa: Nyama iliyonse iziyenda<br />
mmene ikufunira. Nyama ya ndewu sikufunika.<br />
Nthawi iliyonse mukhoza kubwera kwa ine<br />
kudzadandaula. Anthu anga sadzapha ngakhale<br />
mmodzi wa inu moti akafuna nyama azipha ziweto za<br />
m’mudzi osati inu ayi.”<br />
Mkango: “Pepani mfumu tikuduleni pakamwa, ine ndi<br />
anzangawa takondwa kwambiri ndi zimene<br />
mwanenazi. Ine ndilape pamaso panu lero. Ngati<br />
mumaona anthu ena akujiwa, kudyedwa, mtsogoleri<br />
wake adali ine. Kuyambira lero, taleka chifukwa taona<br />
mtima wanu wamlerakhungwa.”<br />
Kalulu: “Tonsefe tiyeni pamodzi tikondwere tipereke<br />
kwa Mfumu Chifuyo, Hepu! Hepu!”<br />
Nyama zonse: “Huree! Hureeeeeeeee!”<br />
Tsopano msonkhano utatha nyama zidakondwera<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
272
koposa poona kuti ufumu wa Chifuyo udaposa<br />
maufumu akale monga ufumu wa a Mkango<br />
womangokudya nawo anzawo, komanso ufumu wa a<br />
Njovu womangopondereza anzawo monga a Kasenye<br />
ndi a Chule.<br />
Nyama zonse ngakhalenso Njokambala ndi<br />
Mkangombala palali kuvomera kuti Mfumu Chifuyo<br />
adzafere m’manja mwawo.<br />
Mfumu Chifuyo tsopano idaganiza zoika nduna zake.<br />
A Njovu ndi amene anasankhidwa kukhala nduna<br />
yaikulu pakati pa nduna zonse. M’nkhalango mudali<br />
chiphokoso cha chikondwerero cha zimene Mfumu<br />
Chifuyo inachita. Tsopano Njovu inasamuka kuchoka<br />
kunkhalango n’kumakhala kwa Mfumu Chifuyo kuti<br />
ikayambe udindo watsopanowo.<br />
Mwadzidzidzi, padamveka kuti Mfumu Chifuyo idapita<br />
koyendera dziko lake ndipo adakumana ndi<br />
Mkangombala ndi Njokambala ndipo zilombozi<br />
zidayamba nkhondo ndi Mfumu Chifuyo. Mwatsoka<br />
Mfumu Chifuyo sinatenge zida za nkhondo ndye<br />
idalumidwa koopsa. A Njovu atamva zimenezi<br />
anathamanga nakanyamula Mfumu Chifuyo pamsana<br />
pawo kupita nawo kunyumba. Kenako a Njovu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
273
anaitanitsa msonkhano wa nyama zonse:<br />
“Ndakuitanani ndine. Onani Mfumu Chifuyo ili gonee.<br />
Ndiyesa mwamva zimene Njokambala ndi<br />
Mkangombala achita. Mfumu ngati iyi sitidzaionanso.<br />
Taonani ine mpando umene adapatsa ife nyama za<br />
m’tchire! Tidali yani kale ife? Siuja tinkangophedwa?”<br />
Nyama zonse zinali ndi chisoni, nthawi imeneyi n’kuti<br />
Njokambala ndi Mkangombala atanjatidwa kale ali<br />
m’ndende ndiponso mapiko awo atadulidwa kale ndi<br />
asilikali. Panamveka mawu akuti Nduna Njovu<br />
ikufunidwa ndi Mfumu yodwalayo.<br />
Mfumuyo inati, “Iwe Nduna Njovu waona chipongwe<br />
chimene wachita Njokambala ndi Mkangombala. Ine<br />
ndidzayesa kubweretsa mtendere pakati pa anthu ndi<br />
nyama, koma mtendere udzavuta mpaka m’tsogolo.<br />
Kumbukirani udani wa munthu ndi njoka kuyambira<br />
pachiyambi. Ine ndimafuna kukonza chidani chimene<br />
chija, koma ndaona chimene adanena Chauta palibe<br />
munthu akhoza kusintha. Ine ndikafa, iwe monga<br />
nduna yaikulu, udzasankha yani kuti adzalowe ufumu<br />
wanga?” Nthawi yomweyo Mfumu Chifuyo inamwalira<br />
koma mawu amene idasiya anali akuti, Ufumu<br />
umenewu adzatenge ndi Mlenje monga mmene Mfumu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
274
inalili. Njovu sinali Mlenje ndipo inadziwiratu kuti<br />
Ufumu wa Chifuyo sadzalowa ngakhale anali nduna<br />
yaikulu. Koma anawuza anthu kuti alenje onse<br />
akufunika ndipo nyama zonse zisonkhane zidzamve<br />
mawu.<br />
Nyama zonse zinatchera makutu kuti zimve mawu a<br />
Nduna Yaikulu. “Zachisoni, Mfumu yathu imene<br />
timaikonda yapita kumanda kosabwerako. Onani<br />
mpando uwu wachifumu, lero ulibe mfumu yake.<br />
Pomwalira mfumu inandiuza kuti, mfumu yotenga<br />
mpando umenewu ikhale imene ili katswiri pa ulenje.<br />
Nonsenu mukudziwa kuti ine ngakhale kuti ndine<br />
Nduna Yaikulu, sindine mlenje. N’kadakhala wokonda<br />
ufumu sindikadakuuzani za mawu amenewa ayi.<br />
N’kadangokuuzani kuti kuyambira lero ndine Mfumu<br />
Chifuyo. Koma ndikufuna alenje abwere apa!” Nyama<br />
zonse zinakuwa, “Koma Njati! Ayi koma Kalulu, ayi<br />
koma N’gonaa!” “Chabwino onse abwere kuno,” idatero<br />
Njovu.<br />
Tsiku lina Nduna Njovu inasonkhanitsa nyama zonse<br />
mmawa ndipo inati, “Sindikufuna kupereka ufumu<br />
kwa bwenzi langa ayi! Koma amene angaonetse kuti<br />
ndi mlenje, alandira ufumuwu! Paja mukudziwa kuti<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
275
pali opikisana atatu: Ng’ona, Njati ndi Kalulu. Mmodzi<br />
wa atatuwa adzakhala mfumu ya tonsefe. Ndiye<br />
kudamboku kwapezeka nyama ziwiri zakufa. Kodi ndi<br />
ndani wasodza chotereyu?” Posachedwa padamveka<br />
mawu, “Ndine Bwana!” Adafulumira kuyankha Ng’ona.<br />
Onse aja, adaomba mmanja, kulemekeza Ng’ona,<br />
ndipo ena amayankhula chonong’ona kuti, “He!<br />
Komatu zadziwikiratu kuti ufumu umenewu autenga<br />
ndi Ng’ona! Chifukwa liwiro lamumchenga lifunika<br />
kuyambira pamodzi. Ng’ona ndiye wapita kale<br />
m’tsogolo!”<br />
Zimenezi Kalulu zidamuwawa mtima chifukwa ena<br />
adayamba kunyoza Kalulu, “Iwe timakukonda,<br />
ndiponso ndiwe wochenjera. Koma lero wangokhala<br />
chitsiru chenicheni, kuchenjera kuja n’kwabodza!<br />
Monga zikhale zoona kuti a Ng’ona n’kutenga ufumu<br />
iwe ulipo?” Adatero a Mbidzi.<br />
Usiku Kalulu adapita kukasaka nyama. Mwamwayi<br />
adapha Ntchefu zitatu nabwera nazo m’mudzi muja<br />
naika pakhomo pa a Njovu. Kenako iye anapita<br />
kukagona, koma popita anadzera kunyumba ya<br />
Mbidzi. “Odi! Odiii!” Kalulu adawodira. “Ndiwe ndani<br />
usiku ngati unooo?” Mbidzi inafunsa. “Ndine Kalulu!<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
276
Paja unanena chipongwe, ndapha Ntchefu zitatu,<br />
ndaika kale kwa a Njovu!” Anatero Kalulu. “Wachita<br />
bwino, ka Ng’ona kodi kapose iwe? Ife tikufuna kuti<br />
ufumu uja ukhale wako! Wachita bwino, tionana<br />
mawa.” Anatero Mbidzi.<br />
Mmawa kutacha, Njovu inakusa onse kuti abwere<br />
kunyumba kwake ndipo inafunsa kuti, “Kodi wampha<br />
Ntchefu izi ndi ndani?” Nthawi yomweyo Ng’ona<br />
inaimirira n’kunena kuti, “Ndine Bwana!” Nthawi<br />
imeneyi Kalulu anachedwa kubwera ndipo anadzapeza<br />
anthu akutamanda Ng’ona akuti, “Ayi, inu Bambo<br />
Ng’ona zanu zili kuyenda bwino, ufumuwu wadziwika<br />
kale kuti ndi wanu.” Kalulu adapita kwa Njovu<br />
n’kunena kuti, “Kodi mwaona Ntchefu zimene ndapha<br />
ine usiku?” Njovu inati, “Choka iwee! Kodi ndiwe<br />
munthu wansanje chotere?”<br />
Kalulu adamva Mbidzi ikumufunsa kuti, “Achimwene,<br />
kodi lija mumandiuza madzuloli lidali bodza?<br />
Kuchedwaku ndi manyazi kuti tingakusekeni! Anzanu<br />
a Ng’ona basi akhala mfumu yathu, kwangotsala kuti<br />
awaveke chigwinjiri kaya ndi khoza la mnyanga.”<br />
Posakhalitsa panamveka kuti pali mphekesera yoti<br />
Mfumu Chifuyo sidaphedwe ndi Njokalamba kayanso<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
277
Mkangombala, koma idaphedwa ndi anthu a m’mudzi<br />
momwemo ndiye adapanga bodza kuti aziti, Mfumu<br />
Chifuyo idaphedwa ndi zilombo. Chotero Kalulu ndi<br />
nyama zina zidatenga thupi la Mfumu Chifuyo<br />
n’kukayika pakhomo pa Njovu, naliphimba ndi<br />
masamba. Mmawa kutacha, Njovu inaitanitsanso onse<br />
kuti abwere ndipo inafunsa kuti, “Kodi pakati panupa,<br />
ndiyesa mwadziwa kuti madzulo ano tili kuponya<br />
ufumu wa Chifuyo. Iyi ndi nyama yomaliza<br />
kutsimikiza kuti wotereyu ndi mlenje wofunika<br />
kumuveka makoza awiri awa!”<br />
Anthu onse ndi nyama zonse zinayamba kukuwa,<br />
“Ng’ona! Ng’ona! Ng’ona! Ng’oooooooooooooonaaa!”<br />
Kenako njovu inati, “Mvetserani kaye. Kodi wapha<br />
imeneyi ndi ndani?” “Ndinee! Ndine Bwana!” Inatero<br />
Ng’ona.<br />
Ndiyeno Njovu inati, “Tsopano paja ena<br />
akumasokoneza, kodi alipo wina wotsutsa kuti<br />
nyamayi sadaphe ndi Ng’ona? . . . Eya, zayenda bwino<br />
lero palibe mkangano. Madzulo ano nonse mubwere<br />
kuti tidzalonge Mfumu yathu yatsopano a Ng’ona!”<br />
“Ooooooooooooooo!” Phokoso lachikondwerero<br />
linamveka. Ng’ona inati, “Lero lomwe lino potsiriza<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
278
phwando, iwe Njovu ukhala nduna yanga yaikulu!”<br />
Wagwira ntchito yako bwino!<br />
Pamene Njovu inachotsa masamba aja anali<br />
pamwamba pa nyamawa, nyama zonse zidati, “O! O!<br />
O! Onani zoopsa! Kodi udapha Mfumu Chifuyo ndiwe<br />
Ng’ona?” Ng’ona imvekere, “Hii! Ndikufa!” Waliwutsa<br />
liwiro kuthawira kumadzi, nangoti pamadzi dyuli!<br />
Mumtima mwake inati, “Koma sindidziwa, zimenezi<br />
zachitika bwanji?” Kuyambira pamenepo Ng’ona<br />
inayamba kukhala m’madzi mpaka lero.<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi nduna yaikulu ya mfumu Chifuyo inali<br />
ndani?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti Ng’ona inkaphadi nyama<br />
zija?<br />
3. Nanga anzake anatani pofuna kuikhaulitsa?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
279
Mfumu Yomveka Tambala<br />
Kale Tambala anali mfumu yomveka pakati pa<br />
mbalame zonse, ngakhalenso nyama zakutchire.<br />
Palibe wina amachita mwano kapena kusewera ndi<br />
Tambala. Onse ankamuopa popeza panali mbiri yoti<br />
ali ndi moto pamutu pake ndipo wochita naye<br />
masewera akhoza kutenthedwa. Mbiri imati onse<br />
okhudzidwa ndi motowo, basi imfa imakhala yomweyo<br />
mpaka kupserera. Motowo unali wosenzera pamutu.<br />
Ndiponso amati m’mawa kukacha Tambala<br />
ankatsokomola ndipo nthunzi wa motowo inkaonekera<br />
uli katukatu!<br />
Tambala amati akangoti, “Kokolirikooooo<br />
kwaachaaaa!” aliyense ankadzuka. Akadzatinso,<br />
“Kokolirikooo kwaachaaaaa!” aliyense ankayenera<br />
kuyamba ntchito kuopa kuti akachedwa<br />
angadzam’tenthe ndi moto uja woyaka lawilawi<br />
pamutu pake.<br />
Nyama zonse, ndi Mkango womwe, mbalame zonse<br />
mpaka Kalize kapena Ndakulapsa, zonse zinkaopa<br />
Tambala. Mbalame zinanso monga Ngolomi,<br />
Chiwombankhanga, Nthiwatiwa, Kadzidzi, Katawa ndi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
280
zina zinkaopanso Tambala. Ndiponso nyama monga<br />
Njovu, Mvuwu, Njati komanso zina zotero, nazonso<br />
zinkaopanso Tambala.<br />
Mbiri inamveka kuti wina atawupala moto wa pamutu<br />
pa Tambala, motowo sungazime mpaka wopalayo<br />
atamwalira. Anatinso sufunika nkhuni koma<br />
umangoyaka nthawi zonse. Mvula ikamagwa,<br />
ankanenanso kuti suzima ndipo umafanana ndi moto<br />
wa mphenzi woyaka mvula ili pooo!<br />
Tambala akangolira nyama zonse zimautsa ana awo,<br />
“Ana inu, ukani mfumu Tambala akuti amatumiza<br />
moto wake monga wa mphenzi kwa waulesi ndi<br />
wosamvera iye. Ukani konzekani ndithu<br />
mungatitenthetse.”<br />
Tsiku lina nyama zonse zinasonkhana pamodzi.<br />
Kalulu anati, “Anzathu, moto wa Tambalawu<br />
watiwopsa. Kumbukirani mdani wa moto ndi madzi,<br />
tiyeni kwa a Mvuwu wokhala m’madzi tikafunsire<br />
nzeru.” Atafika Kalulu anati, “Moni a Mvuwu, tabwera<br />
kuti mutipatse nzeru za moto wa Tambala. Kodi<br />
tingakaupale bwanji?” A Mvuwu anati, “Ifenso m’madzi<br />
muno tathedwa nzeru mbale wanga! Bwanji<br />
osapempha a Njovuwo kuti akapale?” Koma poyankha<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
281
a Njovu anati, “Eee! Ndaniyo, ine n’kadawukonda<br />
moyo, phukusi la moyo sakusungira ndi wina! Bwanji<br />
apite ndi a Nyamalikitiwa?” Koma a Nyamalikiti<br />
poyankha anati, “Ine ndiye toto, kodi mphenzi<br />
pakugwa mumaiwonerera? Hee! Pamakhala zoopsa.<br />
Tonsefe pano n’kutheratu psiti! Moto umene uja akuti<br />
ufanana ndi mphenzi.” Nthiwatiwa anati, “Uja ndi<br />
mdzukulu wanga. Ndipitako ndine. Moto wowopsawo<br />
ndikauwupala.” Nyama zonse zitamva mawuwa zinati,<br />
“Ooo! Wolimba mtima a nthiwatiwaaa!”<br />
Mmawa mwake, Nthiwatiwa inanyamuka ulendo<br />
kupita kwa Mfumu Tambala. Mkazi wake anasenza<br />
chipanda cha mowa. Onse anafika pakhomo pa<br />
mfumu Tambala.<br />
Atafika, Nthiwatiwa inati:<br />
Nthiwatiwa: “Zikomo Mfumu Tambala!”<br />
Tambala: “Eee! Lowani m’nyumba muno. Koma<br />
m’nyumba muno lero sadasesemo, akazi anuwa<br />
analawirira kumunda. Khalani pa chikumbapo.”<br />
Nthiwatiwa: “Ndati ndikawone mdzukulu wanga<br />
mfumu.”<br />
Tambala: “Aa! msatero mfumu sikhalapo popanda<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
282
woibereka. Mwachita bwinoo.”<br />
Nthiwatiwa: “Agogo anuwa anakutengerani<br />
kachiphera dzuwa kuti muyese kufewetsa kukhosi.”<br />
Tambala: “Ha! Mwachita bwino agogo, nanga sindiko<br />
kukhala ukuu!”<br />
Tsopano onse anayamba kumwa. Tambala anamwa<br />
kwambiri mpaka anakhuta, nagona tulo pakama<br />
wake. Nthiwatiwa inatenga ndowe yang’ombe naika<br />
pamutu wa Tambala kuti ikolere moto woopsa uja.<br />
Pamene anawona kuti ndowe sikukolera moto,<br />
anayesa kuyikapo udzu, koma zonse zinangoti zii<br />
opanda moto. Tsopano anaika nthenga zake ndipo<br />
anaona kuti sizinapse. Nthiwatiwa inauza mkazi wake<br />
kuti, “Mkazi wanga, wadziwonera wekha, timangowopa<br />
njokaluzi.”<br />
Atabwerera kwawo, anasonkhanitsa nyama zonse ndi<br />
mbalame zomwe, ndipo anati, “Ine ndinapita kuja<br />
munandituma, mboni ndi mkaziyu. Osamaopanso<br />
amene uja. Simoto uli pamutu uja, ndi litcholotcholo<br />
chabe, lidangofiira koma lilibe moto lili zii kuzizira. Ine<br />
ndidalikhudza ndi nthenga zangazi, osapsa.<br />
Ndinayikapo ndowe ya ng’ombe, mpaka udzu, ayi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
283
ndithu osapsa.” Nyama zonse zitamva izi zinati, “Ooo!<br />
Basi mfumu ndiwe!”<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi nyama zinkaopa Tambala chifukwa<br />
chiyani?<br />
2. Kodi nyamazi zinkaona kuti litcholotcholo la<br />
Tambala ndi chiyani?<br />
3. Kodi Tambala ankadzutsa athu pogwiritsa<br />
ntchito lipenga lomveka bwanji?<br />
4. N’chifukwa chiyani Nthiwatiwa inanena kuti<br />
ankaopa njokaluzi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
284
Chifukwa Chake Kadzidzi Amayenda Usiku<br />
Kalekale ku Chitimbe kumene kunali tchire la bango<br />
lokhalokha, Kadzidzi anali mfumu yoopsa. Mbalame<br />
zonse zinkagwadira iyeyo. Tsiku lina Kadzidzi<br />
anaitanitsa msonkhano.<br />
Pamsonkhanowo Kadzidzi anati, “Zikomo kuti<br />
mwabwera mwaunyinji chonchi, ine ndakhala nanu<br />
zaka zambiri muno m’Chitimbe. Palibe wina<br />
amadandaula. Ndamva kuti Mleme komanso<br />
Nthiwatiwa sakufuna kubwera. Ine monga mukudziwa<br />
ndine mfumu, tsopano ndikufuna banja lililonse<br />
lindipatse thumba la chimanga popeza malipiro anga a<br />
ufumu ndi omwewa.” Mbalame zonse zinati, “Zikomo<br />
mfumu! Mulandira zimene mwanenazo. Koma nanga a<br />
Nthiwatiwa ndi a Mleme, kodi muchita nawo chiyani?”<br />
Kadzidzi anati, “Taonani mbali iyo, mukuona chiyani?<br />
Kodi si asirikali anga amenewa? Uyo wamkulu<br />
mimbayo ndiye mkulu wankhondo ndipo dzina lake<br />
ndi Fwipi. Ali kumbuyo kwakeko ndi Soka, nayenso<br />
ndi wodziwa za nkhondo. Onsewa ali ndi mipando,<br />
kaya udindo wa usajeni ali ndi thepe zitatu. Uyo ali<br />
chakunoyo pampandopo dzina lake ndi Apolo,<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
285
wachiwiri ndi Zenu, wachitatu ndi Tibo amene ali<br />
womalizira pa ulemu wa ankhondo anga. Ndanena izi<br />
kuti mukamva kuti a Mleme ndi a Nthiwatiwa<br />
zawavuta, mudziwe kuti nkhondo yake ndi imeneyi.”<br />
Inu nonse mukachita mwano, nkhondo ya ine Kadzidzi<br />
ndi imeneyo yolamulidwa ndi Sajeni Fwipi.<br />
Wolamulira ankhondo a Mfumu Kadzidzi, yemwe anali<br />
Sajeni Fwipi, ananyamuka ulendo wopita kwa Mleme.<br />
Atafika, Sajeni Fwipi analamula, “Apolo! Gwira Mleme!<br />
Mleme uyo! Akalimbalimba ipha!” A Mleme adagwidwa<br />
n’kutengeda ukaidi. Kenako anauyamba ulendo<br />
wopita kwa a Nthiwatiwa. Atafika, Sajeni Fwipi<br />
analamula, “Apolo! Gwirani msanga Nthiwatiwa uyoo!<br />
Akachita mwano, iphani!” A Nthiwatiwa nawonso<br />
adagwidwa n’kutengedwa ukaidi, ulendo wopita nawo<br />
kwa Mfumu Kadzidzi.<br />
Mfumu Kadzidzi ndi mbalame zonse panali<br />
kukondwera chifukwa cha kulimba mtima kwa Sajeni<br />
Fwipi, Sajeni Soka, Kopolo Apolo, Kopolo Zenu ndi<br />
Kopolo wang’ono Tibo pobweretsa achipongwe aja,<br />
odzikuza. Atafika nawo panali nkhani.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
286
Kadzidzi: “Kodi iwe Nthiwatiwa, bwanji sunabwere ku<br />
msonkhano? Sukudziwa kuti ine ndine mfumu?”<br />
Nthiwatiwa: “Zimenezo mukudziwa ndinu. Kodi si<br />
paja nyama zomwezi ndi zimene zidaveka ine ufumu?<br />
Kodi amene anakapala moto kwa Mfumu Tambala<br />
ndinuyo? Kodi mbalame zinazi sizikudziwa zimenezi?<br />
Funsani a Njovu kapena a Mvuwu akuuzani za ine!”<br />
Tsopano nkhani inavuta popeza mbalame zonse<br />
zidakumbukira za ufumu wa a Nthiwatiwa.<br />
Mleme: “Ine ndidamva moipa. Msonkhanowu amati<br />
ndi wa mbalame zokhazokha, kodi ine ndine<br />
mbalame? Kodi mbalame imakhala ndi mchira? Kodi<br />
mbalame imakhala ndi makutu? Kodi mbalame<br />
imakhala ndi pakamwa, mphuno ndi maso ngati<br />
mmene ndikuonekera inemu? Nanga miyendo yanga,<br />
kodi ikufanana ndi ya mbalame? Kodi ndili ndi<br />
nthenga ngati mbalame nonsenu? Eeeee?”<br />
Mfumu Kadzidzi idakanika kuyankha mafunso a<br />
Mleme ndipo zinali zochititsa manyazi zedi.<br />
Powafukula a Mfumu Kadzidzi, adasowa chochita<br />
ndipo panali umboni wokwanira wosonyeza kuti a<br />
Nthiwatiwa ndi amene anali Mfumu ya Mbalame<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
287
zonse. Ufumu wa a Kadzidzi unali wobera. Akadzidzi<br />
popsa mtima analamula ankhondo ake kuti aphe a<br />
Nthiwatiwa ndi a Mleme. Koma Sajeni Fwipi anati, “Ine<br />
kuyambira lero sindidzakuonaninso ngati mfumu.<br />
Ndiponso Sindingaphe m’bale wanga Mleme ayi.”<br />
Mbaleme zonse zinamuukira Kadzidzi ndipo nthawi<br />
yomweyo anathawira kuthengo. Kuyambira tsiku<br />
limenelo, a Kadzidzi amayenda ndi usiku kuopa<br />
kuonetsedwa mbwadza ndi mbalame zija.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi amene anali woyenera kukhala mfumu<br />
anali ndani?<br />
2. N’chifukwa chiyani Nthiwatiwa komanso Mleme<br />
sizinabwere kumsonkhanowu?<br />
3. Kodi zifukwa zimene anapereka zinali<br />
zomveka?<br />
4. N’chifukwa chiyani Kadzidzi amayenda usiku?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
288
Mkango ndi Bulu<br />
Kalekale Mkango utasowa nyama unasiya ana ake<br />
n’kupita kukasaka nyama. Koma Mkango sunasiyire<br />
ana akewo nyama yokwanira. Ndiye popita, unadzera<br />
kwa bwenzi lake Bulu.<br />
“Bwenzi langa, ine ndikupita kosaka, uzindionerako<br />
ana anga,” unatero Mkango. “Kodi mwawasiyira<br />
chakudya chokwanira?” Anafunsa Bulu. “Ayi<br />
n’chochepa, koma sindikakhalitsa,” unayankha<br />
motero Mkango ndipo kenako unauyamba ulendo<br />
wake.<br />
Patapita tsiku limodzi, Bulu anaona kunjira kuli zii.<br />
Patatha Sabata, Bulu mtima sanaupeze poganiza za<br />
ana a bwenzi lake Mkango.<br />
M’mawa wa tsiku lina, Bulu ananyamuka ulendo<br />
wokaona ana a mnzake. Pamene ankatulukira<br />
pamtunda, anadabwa kuona gulu la anyani pakhomo<br />
pa a Mkango, ana a Mkango ali m’manja mwa a<br />
Nkhwere, ndipo anafunsa kuti, “Kodi Anyani inu,<br />
munayamba kukhala ndi ana a Mkango?”<br />
Nyani wamkulu dzina lake Ziyenda anayankha kuti,<br />
“Kodi iwe Bulu wopanda nyanga, iwe ndiye mlonda wa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
289
a Mkango? Ana awa ife tatenga. A Mkango adayamba<br />
kale kudya ana athu. Ndiye lero tidya ana ake,<br />
kuphanga kwathu kotchedwa Dyero kuli phwando<br />
lero!”<br />
Bulu: “Kodi phanga limeneli lili kuti?”<br />
Ziyenda: “Waona phiri lili apolo? Yang’ana<br />
chakum’mawa kwakeko, kumeneko ndiye kuli phanga<br />
lathu, ubwere ndithu udzadye nawo.”<br />
Bulu: “Chabwino ndibwera, komanso mundikomere<br />
mtima ndibwere ndi mwana wanga wodwala.<br />
Asing’anga a Kalulu anati akudwala matenda a njala,<br />
ndiye atadya nawo phwandolo, akhoza kuchira.”<br />
Ziyenda: “Abwere ndithu.”<br />
Bulu: “Kodi kaphedwe ka mwana wa Mkango<br />
mumakadziwa?”<br />
Ziyenda: “Ayi!”<br />
Bulu: “He! Zikundu zanuzi zikhoza kunyeka zilonda,<br />
moti simungamathenso kukhala pansi. Chabwino,<br />
mundidikire ndidzaphe ndine!”<br />
Ziyenda ndi anzake anavomereza kuti amene adzaphe<br />
ana a Mkango ndi Bulu. “Chabwino, tatsogola<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
290
kukakonzeka. Udzapeza nkhuni zili ndu! kudikira iwe<br />
ndi mwana wako akudwalayo.”<br />
Pamene Bulu ankabwerera kwawo, anakumana ndi<br />
Mkango.<br />
Mkango: “Kodi m’bale wanga Bulu, watani? Nkhope<br />
yakoyi ngati ndi yokondwa!”<br />
Bulu: “Pepani ndithu kwagwa nkhondo. Ana anu onse<br />
awiri atengedwa ndi Ziyenda ndi anzake, anyani aja<br />
amakhala paseri pa phiri iloo!”<br />
A Mkango atamva zimenezi analira, “Vuuu! Vuuu! Ana<br />
anga ineee! Vuuu!” Koma a Bulu anati, “Musalire,<br />
zonse ndakonza kale.”<br />
Tsopano a Bulu analongosola zonse zimene<br />
zinachitika. Anafotokoza mmene anapezera Anyaniwo<br />
akutenga ana a Mkango. “Pepani bwenzi langa, ine<br />
ndawatchera msampha, lero lomwe ana anu<br />
tikawapeza ali moyo.” A Bulu analongosola zonse<br />
zimene adapangana ndi Anyani aja. “Inuyo<br />
ndikuberekani ngati mwana, ndipo tikafika kumene<br />
kuli ana anu. Tikakafika, mukhoza kukachita<br />
chilichonse chomwe mukuona kuti ndi chabwino!”<br />
Anatero a Bulu.”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
291
Atafika, Bulu anati, “Odi! Odi! Ndafika ndi mwana<br />
wodwala uja!” Ziyenda namuyankha kuti, “Lowani.<br />
Ana a Mkango aja ndi awa. Tikudikira kuti muwaphe<br />
kuti tiyambepo phwando lathu. Mwachitanso bwino<br />
kubwera ndi mwana wanu wodwalayu.”<br />
Nthawi yomweyo Bulu anati: “Dzimvere ntolo mwana<br />
wodwala! Zidze pano n’zatonse! Kadziwa mwini nkhuto<br />
wa Fulu!” Kenako a Mkango anatsika pamsana wa a<br />
Bulu. Anyani ataona kuti ndi Mkango, anadziwa kuti<br />
zinthu zasolobana. Anayesetsa kuthawa koma<br />
zachisoni, onse anagwidwa n’kuphedwa ndi Mkango.<br />
Ndiyendo a Mkango anati, “A Bulu, sindinkadziwa kuti<br />
ndiwe munthu wabwino chonchi! Ndiwe bwenzi langa<br />
la pamtima. Taona ana anga onse ali bwino. Tiyeko<br />
kumudzi ndikakupatse mphatso.”<br />
Atafika kumudzi, Mkango unati, “Kuyambira lero,<br />
uzigona m’nyumba kapena m’khola. Sudzagonanso<br />
pabwalo ngati nyama zina zonsezi.”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
292
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Anyani anagwira ana a<br />
Mkango?<br />
2. Kodi Bulu anawauza zotani?<br />
3. Kodi zinali zoona kuti anyani aja akapha<br />
mwana wa Mkango zikundu zawo zikhoza kunyeka<br />
zilonda?<br />
4. N’chifukwa chiyani Bulu anasiya kukhala<br />
m’tchire?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
293
Nkhuku ndi Nkhumba<br />
Tsiku lina Nkhumba inapita padzala. Nkhumbayi inali<br />
n’cholinga chokatoleza zakudya zotayidwa. Dzala<br />
limeneli linali la nyumba ya a Kamzati pamudzi wa<br />
Mawoneka. Pamene Nkhumba inkapita padzalalo,<br />
Khoswe n’kuti ali pompo kale, ndipo ataiona<br />
Nkhumbayo anabisala. Tsopano Nkhuku inabwera<br />
n’kuyamba kukambirana ndi Nkhumba.<br />
NKhuku: “Kodi Nkhumba, bwanji umavutika ndi<br />
zakudya za m’dzala ngati izi? Sizikutsegula m’mimba?”<br />
Nkhumba: “Inetu ndatha masiku ambiri mbuye wanga<br />
osandipatsa chakudya. Zikumveka kuti njala yalowa<br />
kudziko kuno.”<br />
Nkhuku: “Zoonadi, zimene mwamvazo n’zoona.<br />
Chimanga kulibe, gaganso kulibe.”<br />
Nkhumba: “Nanga iwe mnzanga umadya chiyani?”<br />
Nkhuku: “Ndimadya uchi wozuna.”<br />
Nkhumba: “Kodi uchiwo amakupatsa ndani?”<br />
Nkhuku: “Ine ndine wanzeru, bwenzi langa lina<br />
linandipatsa msampha wokolera njuchi ndipo zimaika<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
294
uchi mumsamphawo. Msamphawo umatchedwa<br />
mng’oma. Njuchi zimalowa m’menemo n’kuikamo zisa<br />
za uchi.”<br />
Nkhumba: “M’bale wanga, bwanji ukhale mnzanga?<br />
Ndigawireko uchiwo, taona ine mnzako ndikufa ndi<br />
njala! Taona nthitizi.”<br />
Nkhuku: “Mawa ukonzeke. Koma udzalawire chifukwa<br />
tidzayenda ulendo wautali kuti tikafike kumene kuli<br />
uchiwo. Ndiye popeza mng’omawo uli mumtengo,<br />
ndidzakuuza mmene udzachitire.”<br />
Tsopano Nkhumba inali ndi chimwemwe chodzadza<br />
tsaya itamva zimene nkhuku inamuuza. Koma Khoswe<br />
anabisala uja anamva nkhani yonseyi. Khosweyo<br />
anachita nsanje chifukwa nayenso njala inali<br />
itamuchita kanthu. Zimene ankaba usiku m’nyumba<br />
ya a Kamzati, sizinkapezekanso chifukwa cha njala ija.<br />
Khoswe mumtima mwake anati, “Hee! Tiona, ine<br />
sindingafe ndi njala Nkhumba itapeza mwayi wokadya<br />
uchi. Ndipita nawo komweko. Ndikulakalaka kutacha<br />
msanga kuti nanenso ndikaulawe.”<br />
Mmawa kutacha, Nkhuku ndi Nkhumba zidakumana<br />
padzala paja.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
295
Nkhumba: “Wadzuka bwanji bwenzi langa! Inetu<br />
ndafika kalekale pano. Paja akuluakulu adati, ‘Wamva<br />
m’mimba ndi amene amatsegula chitseko.’”<br />
Nkhuku: “Bwenzi langa, ndasangalala kuti<br />
wandilonjera chonchi. Koma tisachedwe, tiye<br />
tiuyambe. Pajatu ndinati uchiwo uli mumtengo! Ndiye<br />
. . .”<br />
Nkhumba: “Nanga ine ndikakwera bwanji<br />
mumtengowo. Inetu ndilibe mapiko ngati iwe!"<br />
Nkhuku: “Ayi inu a Nkhumba, musandidule<br />
pakamwa. Ndakuuzani kuti lero mukadya uchi,<br />
musakayikire iyayi. Nzeru zili ndi ine.”<br />
Nkhumba: “Ha! Ha! Ha! Lero kuli kudya!”<br />
Nkhuku: “Tamvera bwenzi langa. Ndikuuziretu, pali<br />
lamulo limodzi. Ine ndi iwe titenga nsungwi yaitali,<br />
ndiye iweyo ulume mbali imodzi, ine mbali inayo. Ine<br />
ndigwira ntchito youluka, ndipo iweyo unyamuka<br />
nawo limodzi. Tikafika mumtengomo, usakalankhule<br />
ndi wina aliyense. Ichi ndi chinsinsi chodyera uchi,<br />
timadya koma osalankhula. Koma wamvetsa za<br />
lamuloli?”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
296
Nkhumba: “Zamveka, ndikuona kuchedwa kwambiri<br />
kuti tinyamuke.”<br />
Pamene ankayankhula izi, Khoswe wa padzala uja<br />
ankangomvetsera. Tsopano Khosweyo anathamanga<br />
kwa bwenzi lake Khoswe wa patsidwi kukafunsa<br />
nzeru. Khoswe wa patsindwi anamuuza kuti,<br />
“Nkhumba imene ija ndi mdani wanga. Iweyo<br />
uwalondole, ndiye popeza wamva kale chinsinsi<br />
chawo, iwe upite n’kukaima patsinde la mtengowo.<br />
Uzikachita zinthu zoti zikamupsetse mtima. Ukaona<br />
akagwa n’kufa.”<br />
Mmawa kutacha, Nkhumba ndi Nkhuku zinayamba<br />
ulendo wawo. Zitafika pamtengo uja, Nkhuku inati:<br />
“Waona, mtengo uja ndi uwu. Mng’oma uja ndi uwo!<br />
Tsopano luma nsungwiyo. Konzeka m’bale wanga,<br />
limba mtima, tiye tsopano!”<br />
Nkhumba itaona kuti yakwera mumtengo inasangalala<br />
kwambiri, ndipo nkhuku inatenga uchi uja n’kuipatsa<br />
Nkhumba ndipo onse anayamba kudya. Mwadzidzidzi,<br />
pansi panamveka mawu a Khoswe, “Ha! Chitsiru iwe<br />
Nkhumba wodya zowola, tsika! Kadye zowola zako<br />
kudzala! Tsika chitsiru iweeee!”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
297
Nkhumba inamva izi, mtima wake unayaka moto<br />
ndipo inaiwaliratu lamulo lija loti asamayankhule<br />
akudya uchi. Kenako inati, “Aaa! Kamwana ngati iwe<br />
sungandichite chipomwe chotere. Kodi ndikudya<br />
zako?” Mawu amenewa ali m’kamwa, nthambi ya<br />
mtengo umene Nkhumba inakhala inakhadzuka ndipo<br />
Nkhumba inakuwa kuti, “Hi! Bwenzi langa ndikufa!”<br />
Nkhumba inagwera pansi kuti phii!<br />
Nkhuku itaona zimene zinachitkazo inati: “Oooo!<br />
Bwenzi langa tsokalo, tsokaloo!”<br />
Kenako Khoswe anapita pamene panagwera Nkhumba<br />
paja n’kunena kuti, “Ndinakuuza ndiwe chitsiru,<br />
tachionani chatsakamuka chili gaada! Chimati chitani<br />
chikadya za m’dzala!”<br />
Nkhumba idagwa ndi chipumi moti mphuno yake<br />
idanyindukiratu. Mphuno ya nkhumba inaonongeka<br />
kwambiri chifukwa cha dyera la uchi komanso<br />
kusamvera malamulo.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
298
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani nkhumba inakwera<br />
mumtengo?<br />
2. N’chifukwa chiyani mphuno ya nkhumba ndi<br />
yophwanyika?<br />
3. Kodi dyera komanso kusamvera malamulo<br />
kumabweretsa mavuto otani?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
299
Ng’oma ya Kalulu<br />
Kalulu adali ndi bwenzi lake lapamtima. Bwenzi lakeli<br />
linali Nkhandwe. Tsiku lina Kalulu anaona bwenzi<br />
lakeli likubwera potero. Pa nthawiyi Kalulu ankaotha<br />
moto ndipo n’kuti dzuwa likulowa. Bwenzi lake lija<br />
litafika, Kalulu anakondwa kwambiri ndipo anakonza<br />
zakudya kuti bwenzi lake lisangalale.<br />
Atatha kudya Chakudya, Kalulu anati, “Kodi<br />
mwangotiyendera?” “Ayi bwenzi langa, ine<br />
chandiyedetsa ndi chinthu. Koma ndisanayambe<br />
kulongosola, ndikufuna undiuze mayina a adani ako<br />
onse.” Inatero Nkhandwe. Inkafuna kuti iitane adani a<br />
Kaluluwo kuphwando kuti adzawakhaulitse.<br />
Tsiku la phwandolo litakwana, Njovu, Mkango ndi<br />
Kadyamsonga zidafika kunyumba kwa Kalulu.<br />
Madyerero anayambika, ndiye popeza nthawi idali<br />
itatha, onse adagona. M’mawa kutacha, phwando<br />
linayambanso.<br />
Nkhandwe: Akuluakulu, phwando likayamba, Kalulu<br />
atenga ng’oma iyo n’kuyamba kuimba ndipo tonse<br />
tizivina!<br />
Njovu: Eya! Ilitu ndiye phwando, lochita kuthudzulira<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
300
gule! Nanga paphwando pazichita kukhala ngati<br />
pamaliro?<br />
Mkango: Ndipo inuu! Tiyeni timasuledi ziuno! Mwina<br />
zingachoke dzimbiri.<br />
Kadyamsonga: Koma ndiyetu timuponda gule!<br />
Kenako anapatsidwanso nsimba yangati phiri ndipo<br />
akuluakuluwa anakhala moizungulira. Anaipwekeka<br />
koopsa moti onse anakhuta mimba tugululu, ndipo<br />
anapempha Kalulu kuti ayambe kuwaimbira ng’oma.<br />
Kalulu atayamba kuimba ng’omayo, nyama zonse<br />
zinayamba kuthimbwidzika, nthawi yomweyo Njovu,<br />
Mkango ndi Kadyamsonga, adangozindikira kuti<br />
ayamba kumira m’nthaka ngati kuti ali pamadzi.<br />
Pamene Kalulu anaona zimenezi analimikira kuimba<br />
ng’oma ija. Apono ndiye zinthu zinavuta.<br />
Njovu: Iwe Kalulu, tipulumutse, taona tikumira<br />
munthaka.<br />
Mkango: He! Kalulu, pepa, tipulumutse chonde<br />
tikumira m’nthaka.<br />
Kadyamsonga: Pepa! Pepa Kalulu, Kaluluuuu!<br />
Tipulumutse chondeeee!<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
301
Kalulu: Hehee! Ndiwedi bwenzi langa Nkhandwe!<br />
Waziona mfitizi, zatha lero! Ndizionetsa polekera.<br />
Nkhandwe: Imbitsa! Imbitsa! Imba m’bale wanga<br />
akhaule amenewa!<br />
Njovu: Mayo! Mayoooooo! Tikufa kunoooo! Kalulu,<br />
ndakweza manja anga ndagonja!<br />
Mafunso:<br />
1. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Kalulu<br />
anaitana nyama zija?<br />
2. Kodi n’chiyani chinachititsa kuti nyamazi<br />
zimire munthaka?<br />
3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
302
Ubwenzi wa Njovu ndi Mkango<br />
Kalekale kunkhalango yotchedwa Kambirira pafupi ndi<br />
midzi ya m’dziko la Kabango kunali nyama ziwiri<br />
zokondana kwambiri. Nyamazi zinali Mkango ndi<br />
Njovu. Munkhalangoyi munalinso nyama zina zambiri.<br />
Komabe Mkango nthawi zonse unkangokhala<br />
wachisoni chifukwa unali wokalamba moti unkasowa<br />
mphamvu zogwirira nyama. Nthawi zambiri<br />
unkangokhalira kugona nayo njala chifukwa chosowa<br />
chakudya. Mwamwayi unali ndi bwenzi lake Njovu.<br />
Kawirikawiri Njovu inkapereka mphatso ya nyama kwa<br />
Mkango.<br />
Mkango unkatenga chitete m’mamawa kuli mbuu,<br />
ulendo kukaba maungu m’minda ya anthu. Madzulo<br />
unali ulendo kukapereka maunguwo kwa bwenzi lake<br />
Njovu.<br />
Mwatsoka, chaka china kunasowa mvula ndiye<br />
zachisoni, kunali njala ya mtima bi. Tsiku lina Njovu<br />
ndi Mkango anayamba kukambirana. Mkango unati,<br />
“Bwanawe Njovu, ine masiku ano ana anga akufa ndi<br />
njala. Pakadapanda iwe, tonse bwenzi tili mitembo.”<br />
Koma zinthu zafika posauzana chifukwa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
303
chimkukuluzichi chagwedeza aliyense. Koma kaya<br />
chaka chino tigwira mtengo wanji? “Pepa bwenzi<br />
langa. Chimkukuluzi changati chimenechi ine<br />
ndinachionaponso, ndikuganiza kuti pa nthawiyo<br />
n’kuti iwe usanabadwe. Nthawi imeneyo agogo ako<br />
ndidawaona akudya msipu. Ndipo atete anga<br />
ndidawaona ndi maso angawa akudya nyama. Ndiye<br />
zimene zatigwera chaka chinozi ndikuona kuti<br />
zikulondola mapazi omwewo. Ayi, tiona mmene<br />
zithere. Zikomo!” Inatero Njovu.<br />
Atalekana aliyense anaona msana wa njira. Mkango<br />
utayenda pang’ono unadzera njira yachidule yodutsa<br />
m’tchire. Mwadzidzidzi utatulukira pena unangoona<br />
chimunda cha maungu chili thee! Maungu ali<br />
ngundangunda. Nthawi yomweyo unalankhula<br />
chamumtima nuti, “Ndibwerere ndikauze bwenzi langa<br />
kuti laponda diwa la mphawi, kuli maungu uku!”<br />
Mkango unabwereradi ndi liwiro loopsa. Kenako,<br />
unaona Njovu ikupita potero ndipo unati, “Eeeyi, Ima<br />
pomwepo bwenzi langa ndakupezera maungu!”<br />
Pamene Njovu inamva mawu amenewa inatembunuka<br />
niti, “Kodi n’zoona zimenezo?” Kenako Njovu inayamba<br />
ulendo wopita kumene kunali munda wa maungu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
304
kuja. Atafika pamtunda pamene amapenukira<br />
kumatsitso kumene kunali munda kuja, Njovu inaona<br />
kuti ndi zoona, nkhani ya maungu ija inalidi yoona<br />
ndipo inati, “Zikomo ndithu bwenzi langa,<br />
wandipulumutsa! Tsopano ndithamange liwiro loopsa<br />
kuti ndikapeze mtendere, mundipeza.” Mosachedwa<br />
Njovu inaliyatsa liwiro lothyola nalo mitengo.<br />
Zachisoni pamene Njovu inafika pamunda paja inaona<br />
kuti maungu onse anali owola kwambiri. Zitatero<br />
m’maso mwa Njovu munayamba kulengeza misozi.<br />
Pamene Mkango unkafika unadabwa kuti bwenzi lake<br />
likulila ndipo unati: “Kodi bwenzi langa ukulira<br />
chiyani?” Njovu inati, “Taona maungu aja ndi owola<br />
okhaokha.” Mkango unati, “Aaaa, kodi ndizo<br />
zachitika? Pepa kwambiri. Ili ndi tsoka. Mdani wathu<br />
ndi amene wawoletsa maungu amenewa.”<br />
Njovu inabwerera kwawo ili ndi njala ndiponso<br />
chisoni. Ulendo uli mkati, Njovu inapeza Njati yakufa<br />
ili gadaaa. Njovu inati ndikauza bwenzi langa kuti<br />
ndamupezera mwayi.<br />
Njovu inaliyala liwiro kuthamangira Mkango.<br />
Posachedwa inafika nipeza Mkango utagona pansi<br />
ukubuula ndi njala ndipo njovu inati, “Bwenzi langa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
305
dzuka, kodi watani?” Mkango unayankha kuti, “Pepa<br />
bwenzi langa, ine ndinakomoka ndi njala. Tsopano<br />
imfa yafika moti miyendo yanga ali m’kamwa mwa<br />
ng’ona. Sindikhala ndi moyo ayi.” Njovu inati,<br />
“Dzukani tsopano, ndakupezerani chinyama cha Njati<br />
cha mafuta noninoni.”<br />
Mkango utangomva mawuwa, unangoti, mbalanganda!<br />
Kudzuka, ndipo unathamangira kumene kunali Njati<br />
kuja. Utafika, unangopeza ntchentche zokha zili<br />
m’matsekera zili ng’waaaa. Anthu auzimba<br />
anaipezerera nyama ija, n’kutengeratu yonse. Njovu<br />
inati, “Pepa bwenzi langa, ona mapazi a anthu awa.<br />
Atenga nyama ija ife tili m’njira.”<br />
Tsopano Mkango lilime lake linasololoka, dovu<br />
n’kumangochucha ndipo kenako unagwa pansi<br />
n’kukomoka. Posachedwa Njovu inayamba<br />
kunjenjemera. Nayonso inagwa pansi n’kukomoka.<br />
Kenako mumsewu munkadutsa chigulu cha anthu<br />
ochokera kumsika. Anthuwa anali atatenga zitete<br />
zodzaza ndi maungu, nyama, ufa, chimanga, dzombe<br />
ndi zina. Chifukwa cha phokoso, Njovu ndi Mkango<br />
zinatsitsimuka, tsopano anamva kuyankhula. Atautsa<br />
mitu yawo, anaona kuti anthuwo anasenza zinthu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
306
zabwino zokhazokha. Njovu inati, “Bwanawe, tapeza<br />
mwayi tsopano. Tisasauke ayi. Tikhalebe chogona<br />
ngati tafa. Tikhoza kuwalanda zinthu atengazi.<br />
Mkango unati, “Khala chete, tsopano mwayi wathu ndi<br />
umenewu.”<br />
Munthu wina anati, “Anzathu, onani Mkango ndi<br />
Njovu zaphana! Lero tapeza mwayi, tiyeni titule<br />
katunduyu kuti tichekerane nyama zakufazi.”<br />
Anthu onse anatula pansi katundu wawo, nayamba<br />
kuthamangira nyama zija. Mkango ndi Njovu,<br />
zinadzukira pamodzi kuti, mbalanganda, mkango<br />
umvekere, “Vuuu! Vuuu!” nayonse njovu imvekere,<br />
“Kherrrr! Kherrr!” Anthu aja amvekere, “Mayo mayo<br />
mayo ineeeeeee! Tikufa kunoooooo!”<br />
Anthu aja atathawa, Njovu ndi Mkango zinakhala<br />
pansi n’kuyamba kudya zimene anthuwo anasiya.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
307
Mafunso:<br />
1. N’chiyani chikusonyeza kuti njala inali itafika<br />
poipa kwambiri?<br />
2. Kodi n’chiyani chikusonyeza kuti Mkango ndi<br />
Njovu zinali mabwenzi okondana kwambiri?<br />
3. Kodi nyamazi zinatani kuti zipeze chakudya?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
308
Kalulu Aphetsa Ana<br />
M’dziko lotchedwa Fukizi munali munthu wina amene<br />
anali wolimbikira kulima mtedza. Munthuyu dzina<br />
lake anali Bikoko.<br />
Mtedza utacha, Bikoko anaona mapazi anyama za<br />
mtchire. Pambuyo, anaona kuti mtedza wake<br />
unayamba kuwonongeka. Nyama zambiri zinali<br />
kuwononga zokolola zake. Nyama zimene<br />
zimawononga sankazidziwa kwenikweni. Motero,<br />
anaganiza kuti akabisale kuti aone nyama zimene<br />
zinali kuwononga zokolola zake. Bambo Bikoko<br />
anakhala m’chisimba chake koma sanaone nyama<br />
iliyonse.<br />
Kalulu anangoti m’munda muja, tulukiru! Maso<br />
mwazumwazu! Kenako anaona mwini munda ali<br />
m’chisimba. Kalulu uja anayenda mochenjera kuopa<br />
kuonedwa ndi mwini munda. Tsopano anatenda<br />
dzungu n’kuliboola, iyeyo n’kulowa m’menemo ndi<br />
kulivundikira bwino kuti wina aliyense asamuone.<br />
Bambo Bikoko anatopa tsopano, ndipo anaganiza<br />
zopita kumudzi kukapumula. Atangochoka, njovu<br />
inafika nitola dzungu lija munali Kalulu, n’kumeza.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
309
Njovu ija ili kuyenda, Kalulu anazindikira kuti ali<br />
m’mimba mwa Njovu ndipo anati, “Lero kuli phwando,<br />
n’kutere zamkati kunona!” Kalulu anatulutsa mpeni<br />
wake n’kudula mtima wa Njovu. Nthawi yomweyo<br />
Njovu inagwa, n’kuferatu.<br />
Tsopano Kalulu ataona kuti Njovu yafa, anatulukira<br />
kukamwa kwake ndipo mosachedwa anatenga mpango<br />
nayinjata nsangamutu.<br />
Nthawi yomweyo Kalulu anaona anthu a uzimba ali<br />
kupha ziwala. Kalulu anakwera pachulu nayamba<br />
kukuwa nati: “He kodi imeneyo ndi nkhuli?” Anthu aja<br />
anamuona Kalulu uja, nayamba kum’thamangitsa,<br />
koma kalulu anazungulira chitsamba, n’kulowa<br />
m’mimba mwa Njovu ija ndipo a uzimba aja atafika<br />
pafupi ndi Njovu, Kalulu anayamba kubuwula. Anthu<br />
aja anayifunsa Njovu ngati inaona Kalulu, koma Njovu<br />
inati: “Pepani abale anga ine sindili bwino ayi. Litsipa<br />
landivuta kwambiri.” Anthu aja anabwerera<br />
osamuowona Kalulu, kenaka, Kalulu anatulukanso,<br />
n’kukwera pachulu chija nati: “Nkhuliyo m’dambomo!”<br />
Kalulu analowanso m’mimba mwa Njovu yakufa ija.<br />
Tsopano anthu aja anatopa naye Kalulu ndipo<br />
anaganiza zoika mlonda kuti aone chinsinsi cha<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
310
Kalulu ndipo anaika mlonda pa chitsamba pafupi ndi<br />
Njovu ija. Anthuwo atachoka, Kalulu anatulukanso<br />
n’kukwera pachulu nati, “Nkhuliyo m’dambomo!”<br />
Atatero anakalowanso m’mimba mwa Njovu ija,<br />
mlonda uja akuona zonse zomwe zinkachitika.<br />
Mlondayo anaona kuti polowa m’mimba mwa njovu<br />
analowera pakamwa ndipo anamva Kaluu akubuula<br />
m’mimba mwa Njovumo.<br />
Mlonda uja anaubutsa ulendo kupita kwa anzake aja<br />
nawauza kuti chinsinsi cha Kalulu chimene<br />
anachipenya. Anaulula kuti Kalulu akumathawira<br />
m’mimba mwa Njovu ndipo akumayamba kubuula,<br />
kutiphimba m’maso kuti tiziti ndi Njovu ili kubuula.<br />
Anzake aja anati, “Hi! Talekerera nyama!” Ndipo<br />
ananyamuka n’kupita pamene panali nyama paja<br />
mipeni ili m’manja kukayamba kucheka nyama ya<br />
Njovu. Kalulu atamva kuti anthu aja ayamba kuicheka<br />
Njovu ija, analimbikira kubuula: “Mayo ine! Ha!<br />
Haaaaaaa! Litsipa ine. Litsipa ineee! Nditani inee!<br />
Kandifunireni mankhwala anthu inu! Ndili ndi moyo<br />
anzanga inuu.” Mlonda uja anati, “Bodza, bodza! Ndi<br />
Chikalulu!”<br />
Pamene Kalulu anamva mawu amenewa, basi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
311
anadziwa kuti zake zada. Tsopano anaganiza nzeru<br />
ina. Iye anati, “Tsopano anthu amenewa anditulukira,<br />
ine zimene ndichite, iwo asanandipeze, ndilowe<br />
m’chifu cha Njovuchi.” Kalulu anabisala m’chifu cha<br />
Njovu.<br />
Anthu aja ataiboola Njovu ija m’mimba, anaona kuti<br />
mulibe Kalulu. Bikoko mtsogoleri wawo anati, “Kodi<br />
iwe mlonda, suja umanena kuti m’mimba mwa Njovuyi<br />
muli Kalulu? Nanga ali kuti?” Mlondayo anati,<br />
“Bwana, ntchito yopeza zinsinsi za Kalulu ikadalipo.<br />
Ine ndapusa koma wopusa sadziwika. Uyu Kalulu<br />
timamudziwa tonse.” Bikoko anati, “Chabwino, ine<br />
udziwa ndimakonda chifu cha Njovu, chifukwa<br />
mumakhala maungu ophikika bwino, chitenge upatse<br />
mwana wanga Bwasano uyo, akapereke kwa amake<br />
kuti akaphike.” Chifu chija anachitenga Bwasano<br />
kupita nacho kumudzi.<br />
Ali panjira, mwana uja anamva kuti chifu<br />
chikuyankhula, “Taya! Taya! Fulumira tayaa!”<br />
Bwasano atamva zotere, zinamudodometsa ndipo<br />
anataya chifu chija n’kuyamba kuthawa.<br />
Nthawi yomweyo Kalulu anatuluka, mwana uja<br />
osadziwa, ndipo anathyola masamba a mtengo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
312
wotchedwa kafwito nasunga m’manja. Munthu<br />
akangotafuna masambawa amagona tulo tofa nato<br />
tsiku lathunthu. Kalulu anauza Bwasano kuti, “Bwera<br />
kuno! Bwera kunooo!” Mnyamata uja anacheuka,<br />
ndipo anabwerera.<br />
Kalulu: Kodi umathawa chiyani?<br />
Bwasano: Chifuchi chimayankhula.<br />
Kalulu: Ayi wayamba misala iwe, tenga mankhwalawa<br />
utafune m’kamwa mwakomo ndiye pafunika kuti<br />
upumule, usayendenso ayi, tsopano lowa m’chifumo<br />
ukakhale pansi, ine ndikunyamula. Ine ndine<br />
sing’anga oposa onse. Lowa msanga!<br />
Bwasano analowa m’chifu chija ndipo Kalulu<br />
ananyamula chifucho ulendo kwa mkazi wa Bikoko.<br />
Atayandikira, Kalulu anafunsira za nyumba ya a<br />
Bikoko, ndipo anauzidwa mmene angakafikire<br />
kunyumbako.<br />
Atatulukira pamudzipo anaona nyumba imene inali<br />
ndi chikwere cha nkhunda pabwalo ndiponso panali<br />
mitengo itatu ya naphini, ndiyeno anati, “Monga muja<br />
andiuzira anthu, nyumba ya Bikoko ndi imeneyi.”<br />
Kalulu anaodira, “Odii! Odii!” Mayi onenepa aafupi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
313
koma oyera, atsitsi la nzindo anatulukira koma<br />
nkhope ili yachisoni.<br />
Kalulu: Kodi Mayi, ndinu amayi a kwawo kwa a<br />
Bikoko?<br />
Mayi: Eee!<br />
Kalulu: Bwanji osakondwera ndi chimtengatenga<br />
ndatengachi?<br />
Mayi: Ayi a Kalulu, ine ndili pachisoni chachikulu.<br />
Kuno kuli matenda banja lonse ngakhale inenso<br />
m’thupimu simwanga ayi. Ana athu awiri Diroli ndi<br />
Chisangwi onse ali gonire, moti a Bikoko ndiponso<br />
Bwasano sakudziwa zimenezi. Ndangokhala ndekha,<br />
ndiye ndangoti ndodo mtolo!<br />
Kalulu: Pepani mayi koma limbikirani kuwafunira<br />
zitsamba zonse zili m’tchirezi. Mayi ine ndatumidwa<br />
ndi Bambo Bikoko kudzatula chimtengatengachi. Iwo<br />
akuti mutenge chimtsuko chachikulu ndipo miyikemo<br />
chifuchi osachidulayi. Akuti muli maungu awo ndipo<br />
akufuna apsere m’chifu chomwechi. Anatero<br />
malamulo awo a chifuchi. Ndiponso akuti mundiphere<br />
nkhuku popeza ndanyamula chifu chawochi.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
314
Amayi aja msangamsanga chifu chija anachiika<br />
m’chimphika chachikulu, naika pamoto. Anaphanso<br />
nkhuku naika mumphika waung’ono. Nsima<br />
inaphikidwa ndipo Kalulu anadya nsima ija ndi nyama<br />
ya nkhukhu. Kalulu anasonkhanitsa mafupa onse<br />
n’kusunga ali, “Chimapulumutsa munthu<br />
sichidziwika.” Kenako anauza mayi aja kuti, “Pepani<br />
mayi ine m’thupimu sindikumva bwino, ndimati<br />
ndipemphe malo ogona.”<br />
Nthawi yomweyo mayi uja anatenga nsalu yakuda<br />
n’kumupatsa Kalulu nati, “Bwerani kuno mugone<br />
pamodzi ndi Diroli ndi Chisangwi, iwe ugone pakatipo.<br />
Mungogonera limodzi popeza mphasa yapadera palibe.<br />
Ndadziwa wadwala chifukwa unanyamula katundu<br />
wolemera kwambiri.”<br />
Kalulu anagona pakati paja nafunda nsalu yakuda<br />
koma Diroli ndi Chisangwi anafunda nsalu zoyera.<br />
Amayi aja ali kusonkhezera mphika uja, chimoto chili<br />
lilili! kuyaka, chimphika chija chili, bwata! bwata!<br />
kubwatitsa chifu cha a Bikoko. Nthawi yomweyo a<br />
Bikoko anafika ndipo anafunsa, “Kodi chifu chafika?”<br />
“Zoona, chifu chafika ndi Kalulu,” anayankha motero<br />
amayi aja. “Aa! Chafika ndi Kalulu! Kodi ine ngati<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
315
ndinatuma Kalulu, ine ndinatuma Bwasano osati<br />
Kalulu ayi,” anatero a Bikoko. “Hi! zanu izooo, Kalulu<br />
ndiye wabweretsa.” Anayankha motero amayi. “Bwanji<br />
waphika motere chifu changa? Kodi chifu amaphika<br />
osafinya? Mkazi wosadziwa kuphika iwee!” Anazaza<br />
motero a Bikoko. “Ndachita motsata malamulo anu,<br />
anandiuza zimenezi ndi Kalulu,” anayankha motero<br />
mayi aja.<br />
Nthawi imeneyi Kalulu ankamva phokoso lija, tsopano<br />
anasuntha malo, anagona kumbuyo kwa Chisangwi,<br />
ndiye kuti Chisangwi, anali pakati tsopano, nsalu<br />
anatenga yoyera ya Chisangwi ndipo Chisangwi<br />
anamufunditsa yakuda ija ali, “Ee! Tione mmene<br />
zikhalire.”<br />
Bikoko: Tenga mpeni toboole chifuchi tichifinye, kuti<br />
tiphikenso bwino.<br />
Mkazi wa Bikoko: Kodi mukufuna kuona maungu<br />
anuwo?<br />
Bikoko: Maungu ati?<br />
Mkazi wa Bikoko: Akuti muli maungu anu mmenemu<br />
n’chifukwa chake mumati tiphike chotere.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
316
Bikoko: Amatero ndani?<br />
Mkazi wa Bikoko: Inuyo! Kodi chifuchi ndimayesa<br />
chachokera kwa inu? Nanga ine ndikadangochita za<br />
m’mutu mwanga?<br />
Bikoko: Zonse n’zabodza, Kaluluyo wapita kuti<br />
ndimufunse.<br />
Mkazi wa Bikoko: Wadwala, wagona pakati pa Diroli<br />
ndi Chisangwi kuchipinda cha ana, wafunda nsalu<br />
yakuda ija.<br />
Bikoko: Phula mphika! Tenga mpeni ting’ambe,<br />
tiphikenso titafinya.<br />
Bikoko anatenga mpeni nang’amba chifu chija. “Ooo!<br />
Mayo! Mayoo! Mwana wangaaa!” Anaona Bwasano<br />
wophikika atafa kale. Amayi anafunsa, “Kodi<br />
n’chiyani?” Bikoko anati: “Hii! Mwana wapsa! Waphika<br />
Bwasano!” Bambo analira. Amayi anathamanga kuti<br />
akaone, “Mayo! Mayo! Mayo! Nkhondoyoo!” Bikoko<br />
anati, “Patse uta wanga! Lero naye akufanso!” Onse<br />
analowa m’chipinda chija.<br />
Mkazi wa Bikoko: Kalulu ndi uyo ali pakatiyo.<br />
Mlaseni!<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
317
Bikoko: Aona polekera lero, ndimukhomerera pansi<br />
ndi muviwu!<br />
Wodwala: Mayo atate mwandipha!<br />
Tsopano Kalulu bzunthu! waliutsa liwiro.<br />
Povundukula nsalu yakuda ija anaona ndi Chisangwi,<br />
ali, thinuuu! thinuuu! kusauka ndi imfa. Bikoko anati,<br />
“Hii! Ndapha mwanaa!” Waliyatsanso liwiro<br />
kuthamangira Kalulu. Tsopano Kalulu anatsekula<br />
liwori lake lomaliza agalu ali taaawaaa! Kalulu anaona<br />
kuti zinthu zavuta popeza agalu ena anamubzola<br />
ndikum’dulizira kutsogolo, Kalulu anatenga mafupa a<br />
nkhuku aja n’kumawatayira, ndiye agaluwo<br />
akadachedwa ndi kulimbirana mafupa iye anangoti<br />
khophe! wapita. Nafenso tiyenera kuchenjera ndi<br />
anthu a maonekedwe ngati a Kalulu.<br />
Mafunso:<br />
1. N’chifukwa chiyani Kalulu analowa m’kati mwa<br />
dzungu?<br />
2. Kodi anapezeka bwanji m’kati mwa chifu?<br />
3. Kodi khalidwe lakeli linaphetsa bwanji ana?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
318
Ubwenzi wa Kalulu ndi Fisi<br />
M’dziko la Nsabwe, munali akazi awiri amene<br />
ankafuna kukwatiwa ndi nyama zam’tchire. Adaganiza<br />
zimenezi chifukwa akaziwa ankaona m’mene akazi<br />
anzawo ankazunzidwira ndi amuna awo. Maina a<br />
akaziwa anali Khumbo ndi Mtimaukanena.<br />
Nyama zam’tchire zinamva za mbiriyi. Posakhalitsa<br />
nyama zamitundumitundu zinayamba kubwera kwa<br />
Nsabwe koma zambiri zinalephera mbeta za akazi<br />
awiri aja. Tsiku lina a Njovu, a Njati ndi a Mkango<br />
adapitira limodzi kukayesa nawo kufunsira mbeta zija.<br />
Njovu: Kodi iwe Mtimaukanena, ine ukandiona,<br />
umandiona bwanji? Sumandigomera? Kodi mwamuna<br />
ukufunayo, amaposa ife a Njovu? Pofuna amuna<br />
muzisankha ife amphamvu, a mangolomera.<br />
Mtimaukanena: Pepani a Njovu. Mtima wanga<br />
sunandiuze kuti ndikuvomereni ukwati ayi.<br />
Njovu: Chabwino, tabwera iwe Khumbo, kodi<br />
ndimayesa kuti mukufuna ife nyama zam’tchire,<br />
tabweratu kwa ife a Njovu. Kodi simukukhutira nane?<br />
Khumbo: Ayi a Njovu, mtima wanga sunakhumbe inu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
319
ayi.<br />
Njovu: Atsikana awirinu, zedi mwataya mwayi, tsiku<br />
ndi tsiku bwenzi mukudya maungu mukanalola ine.<br />
Khumbo: Hoo! Zakuba m’minda mwa enizo! Toto ine<br />
kukwatiwa ndi chimbala! Anthu ambiri anapunduka<br />
chifukwa chakudya zotsirika. Toto ifee!<br />
Tsopano a Njovu anatuluka nauza anzake aja kuti:<br />
“Anzanga, tangovutika, anamwaliwa ndi okongola<br />
koma ndi ovuta. Tangotaya nthawi pachabe kubwera<br />
kuno.” A Mkango anati, “Ine sindingangobwerera<br />
kunjira pokhapokha nane nditayesa mwayi wanga,<br />
zichite kukakanikira komweko.”<br />
Mkango: Odii atsikana, tabwera ife amunamuna, a<br />
Mkango odya nyama tsiku ndi tsiku. Si za aja a Njovu<br />
odya mawungu akuba ayi. A Mtimaukanena,<br />
mukuganiza bwanji za ine? Bwanji ndinkhale<br />
mwamuna wanu?<br />
Mtimaukanena: Pepani a Mkango, mtima wanga za<br />
inu sunanene kuti mukhale mwamuna wanga.<br />
Mkango: Nanga iwe Khumbo? Ukuti bwanji?<br />
Khumbo: Ayi, pepani, mtima wanga sunakukhumbeni<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
320
mpang’ono pomwe.<br />
A Mkango anapsa mtima ndipo anangotuluka<br />
m’nyumba muja. Atafika kwa anzake anati,<br />
“Anzanganu, basi tiyeni tizipita kwathu. Ukaona<br />
mtengo wauwisi ukuyaka, nanga wouma n’kutani?<br />
Kwenikweni inu ongodya msipu mumtsinje, ha!<br />
Sangakuwerengereni n’komwe, akhoza<br />
kukangokutukwananiko. Tiyeni tizipita.”<br />
Mbiri inamveka m’mkhalango yonse kuti zinthu<br />
zavuta. Onse akuluakulu atatu akanidwa ndi mbeta<br />
mochititsa manyazi. Kalulu ndi Fisi anawawidwa<br />
mtima. Tsiku lina Fisi ananyamuka kupita kwa akazi<br />
aja.<br />
Fisi: Zikomo! Zikomooo! Tafika ife amuna osaopa<br />
mdima, oyenda usiku ndi usana. Ndabwera<br />
kudzafunsira ukwati nonsenu, ndikufuna ndikhale ndi<br />
akazi awiri. Nanga muli ndi mawu?<br />
Mtimaukanena: Mtima wanga wanena kuti mwamuna<br />
amene ndakhala ndikuyembekeza ndinu. Ndavomera!<br />
Khumbo: Inenso, mtima wanga wafera inuyo basi! Inu<br />
a Fisi ndiye taona kuti mukhale mwamuna wa ife<br />
awiri.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
321
Fisi: Chabwino, ndikukatenga nkhoswe yanga kuti<br />
tigwirizire chinkhoswe. Sindifuna ukwati wachabe,<br />
wongotengana popanda chinkhoswe ngati amachitira<br />
enawa.<br />
Mbiri inamveka m’nkhalango monse kuti Fisi ndiye<br />
amene waloledwa kukhala mwamuna wa akazi awiri<br />
aja. Nyama zonse zinali zododoma popeza Fisi ndi<br />
wakuba, wodya zoola komanso zakufa. Fisi atafika<br />
kwa Kalulu, anafotokoza monga mmene zinayendera.<br />
Kalulu anavomera kukhala nkhoswe ya Fisi.<br />
Tsiku la Chinkhoswe lisanafike, Kalulu anangolawira<br />
kuti akukasamba kumtsinje, koma unali ulendo<br />
wopitakwa akazi aja. Atafika Kalulu anati, “Tamva kuti<br />
mwalola Fisi kuti akhale mwamuna wanu nonsenu.<br />
Akazi opanda nzeru ngati inu sindinawaonepo. Kodi<br />
simudziwa kuti Fisi amadya zoola, zongofa zokha<br />
komanso ndi wauve koopsa? Simudziwa kuti Fisi ndi<br />
bulu wanga?”<br />
Kalulu: Nanga inu mwafera chiyani? Fisi ndi mbala<br />
yoopsa. Amachita mgoneko usiku ulionse. Mbuzi,<br />
nkhumba za anthu zatha phu! Kuti apeze chakudya<br />
chaufulu, ayi, ntchito ndi kuba m’midzimu. Amene uja<br />
ndi bulu wanga. Kodi simukudziwa zimenezi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
322
Khumbo: Ayi sitidamvepo. Koma inuyo mutitsimikizire<br />
kuti a Fisi ndi bulu wanu. Mukachita zimenezo, ife<br />
tidzasintha mtima ndipo tidzakwatiwa ndi inu a<br />
Kalulu.<br />
Kalulu anabwerera kwa bwenzi lake Fisi. Tsiku la<br />
chinkhoswe linafika, ulendo unali mkati wopita kwa a<br />
Nsabwe. Atatsala pang’ono kufika, anafika pamtsinje<br />
wina. Kalulu anathamangira madzi a mumtsinjewo<br />
n’kuyamba kumwa. Fisi anafunsa, “Kodi ukumwa<br />
madzi nthawi zino bwanji?” Kalulu anayankha kuti,<br />
“Ndiye kuti ndayamba kudwala m’bale wanga,<br />
sindithanso kuyenda ayi. Pepa bwenzi langa,<br />
tifulumire kukatula mbetayi ndiponso lero lomwe<br />
tikagwirire ndithu chinkhoswe. Ine ndine nkhoswe<br />
yako ya kuchimuna. Tsono miyendo yanga, yauma,<br />
sinditha kuyenda. Iwe uyenera kundibereka pamsana<br />
kuti tikafike msanga.”<br />
Fisi anaberekadi Kalulu. Posakhalitsa onse anafika.<br />
Koma atafika pafupi ndi akazi aja Kalulu anauka<br />
n’kuimirira, ndipo anatenga ndodo yake amvekere,<br />
thya! kukwapula a Fisi. “Yenda bulu wanga! Tiye chita<br />
liwiro! Yenda bulu wangaa!” Kenako anayamba kuuza<br />
mbeta zija kuti, “Suja ndidakuuzani madona kuti fisi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
323
ndi bulu wanga!”<br />
Fisi atamva mawu amenewa anangolira, “Uwi!<br />
Uuuuuuuuuuuuuwi! Kalulu ndizo udakonza<br />
zimenezo, tenga akaziwo zako ziyende!” Atatero<br />
anangoti patchire lowu, zii! wapita. Akazi aja anati,<br />
“Zoonadi, a Kalulu samanamayi!” Ndiyeno Kalulu<br />
anati, “Paja ndinakuuzani kuti fisi ndi bulu wanga!<br />
Mwazionera nokhatu!”<br />
Kalulu anakwatira akazi aja, Mtimaukanena ndi<br />
Khumbo. Fisi ndi Kalulu anadana koopsa. Pakati<br />
pawo panali chidani chosamwerana madzi kuopa<br />
kuthirirana mankhwala.<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi n’chifukwa chiyani akazi awiri amene<br />
atchulidwa m’nkhaniyi ankafuna kukwatiwa ndi<br />
nyama zakuthengo?<br />
2. Kodi ndi ndani amene anakanidwa mochititsa<br />
manyazi?<br />
3. Nanga atsikanawa anavomera ndani?<br />
4. Kodi Kalulu anachita chiyani pofuna kulanda<br />
akaziwo?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
324
Kuunika ndi Mdima<br />
Tsiku lina Kuunika ndi Mdima kunayamba<br />
kukangana kuti adziwe amene anali wofunika<br />
kwambiri pakati pawo. Kuunika kunayamba<br />
kuyankhula modzigomera kumvekere, “Eee, ndine<br />
patali, zinthu zonse zimasangalala ndikamawala ndipo<br />
ndine wamphamvu zedi kuposa aliyense. Nditangoti<br />
ndisawale kwa masiku angapo zomera zonse zikhoza<br />
kufa. Anthu akhoza kumavala zovala zaziwisi komanso<br />
kumangopunthwa akamayenda. Kodi anthu otsogola<br />
ndi tekinoloje akanalowera kuti kukapala mphamvu<br />
zoti aunikire midzi yawo. Kunena zoona palibe amene<br />
angafikepo pamene ndinafika ine! Sindili ngati inuyo a<br />
mdima. Kuda muli bii ngati makala, moti umadziwa<br />
zoti pali munthu akatsokomola. Anthu alibe nawe<br />
ntchito, n’chifukwa chake amapala moto kwa ine<br />
n’kumaunikira usiku.” Mdima utamva chipongwe<br />
chimenechi unapsa mtima ndipo unauza Kuwala kuti,<br />
“Pakadapanda ine anthu sakanamaliza mkonono,<br />
bwenzi anthu akumwalira ndi tulo. Akuba sakadapata<br />
chawo chuma komanso Afisi akadavutika koopsa<br />
chifukwa cha njala, nanga adakamatola bwanji<br />
zowola. Iwe kuwala ndiwe woyerekedwa. Kodi sudziwa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
325
kuti anthu amadana nawe? Amati umawawaula,<br />
kuwaononga maso komanso kuwayambitsira<br />
matenda. Amakupherera ndi mwafuli, kuvala mandala<br />
komanso ena amakana kuyenda iwe ukamawala.<br />
Zikanakhala kuti ali ndi mphamvu zokuchotsa<br />
paudindo bwenzi atakuchotsa kalekale chifukwa<br />
anatopa nawe.” Kenako mkanganowo unafika povuta<br />
moti mdima unati, “Tiyeko tipandane tione uyo ali<br />
wadzitho komanso wofunika!” “Chabwino bwera<br />
ndikuphofomole uone,” anatero Kuunika. “Iwe<br />
Kuunika, undipeze madzulo kuti ndidzakuchotse<br />
chimbenene! Panopa ndikufuna ndithandize anthu<br />
kuti apeze ufulu wochita zomwe akufuna.<br />
Umawaphera anthu ufulu iwe! Udzamangidwatu,<br />
zoona ungamayalutse anthu olemekezeka!”<br />
“Chabwino, ndibwera!”<br />
Madzulo, Mdima unadikira mpaka kutopa, koma<br />
kuwala sikunatulukire. Unkangoyang’anira kunjira<br />
maso ali psuu! Tsiku lotsatira Kuwala nakonso<br />
kunadikira mpaka madzulo moti nakonso maso<br />
anafiiriratu psuu, koma sunaone mnzake akubwera.<br />
Usiku unayamba kudzitama umvekere, “Amati atani<br />
Kuunika kapolo? Akuchita mantha kuopa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
326
kupandidwa!” Masana nakonso Kuunika kunayamba<br />
kudzitama kumvekere, “Amati achite chiyani kapolo<br />
amene uja Mdima, wandiopatu!”<br />
Tsiku lina atakumana, ndewu inayamba masanasana.<br />
Nthawi ya madzulo, Kuunika kunagonja n’kugwera<br />
pansi kwalaaa! Mdima utaona zimenezi unati,<br />
“Heheeeedeee! Umati uchite chiyani kamwana iwee!”<br />
Pakati pa usiku, ndewu inabadwa, nthawi ya m’mawa<br />
usiku unagonja. Nakonso kuunika kunayamba<br />
kuseka, “Pwitipwitipwiti! Umati uchite chiyani mwana<br />
woonekera matumbo iwee! Pamenepa mpamene<br />
panayambira udani wawo. Kuunika kunadziwa kuti<br />
mwamuna mnzako mpachulu. Mdima nawonso<br />
unaona kuti mnzakeyo mpachulunso, moti mdima<br />
unkati ukaona kuwala akubwera poteropo, unkachoka<br />
n’kupita kwina. Nakonso kuunika kukaona kuti<br />
Mdima ukubwera, kunkasintha njira kapena<br />
kubwerera kwawo kukagona.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
327
Mafunso:<br />
1. Kodi pakati pa kuunika ndi mdima, chofunika<br />
kwambiri ndi chiyani?<br />
2. Kodi ndi pati pamene panayambira udani wa<br />
kuunika ndi kuwala?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
328
Nzeru za Kalulu<br />
M’nkhalango yotchedwa Ngwangwa m’dziko la Fukuto,<br />
munali nyama zosiyanasiyana. Chaka china mvula<br />
inakanika kugwa moti madzi ankasowa. Mkati mwa<br />
m’nkhalango ya Ngwangwa munali chitsime chimodzi<br />
chokha. Mwachidule tingati chitsimechi chimadziwika<br />
ndi dzina loti Mzizime. Chinali chitsime chamadzi<br />
okoma, ozizira bwino komanso ochotsa chipemba.<br />
Nyama zonse zinkapita kuchitsimechi kukamwa<br />
madzi. Nthawi zina zinkapezeka kuti chitsimechi<br />
chaphwa. Pofufuza, nyama zonse zinatsimikiza kuti<br />
anyani ndi amene ankaphwetsa chitsimecho chifukwa<br />
ankamwa madzi moipa kwambiri. Zitatero, Njovu<br />
inaitanitsa nyama zonse kuti zidzamve malamulo a<br />
chitsime cha Mzizime. “Ndati ndinene pano kuti<br />
anyani asiye kumwa nawo madzi a pachitsime<br />
chathuchi. Ndamva zoti anyaniwa ndi amene<br />
akumaliza madzi pachitsimechi. Choncho kuyambira<br />
lero, muonetsetse kuti anyani asamabwere kuno<br />
kudzamwa madzi! Nkhani imene ndinakuitanirani ndi<br />
imeneyi.”<br />
Njovu inapitiriza kunena kuti, “Iwe Mvuwu, Mbidzi,<br />
Mkango, Kadyamsonga ndi Nyamalikiti, imwani<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
329
madziwa tsopano tizipita. Koma muonetsetse kuti<br />
nyani asadzaoneke pachitsimechi. Amene adzagwire<br />
mbala zikuba madziwa, ndithu adzalandira mphoto<br />
yaikulu. Ine sindisamala za ufumu wanga ayi. Amene<br />
adzagwire mbala ikuba madziwa adzapatsidwa ufumu<br />
wangawu.”<br />
Kalulu anaimirira n’kunena kuti, “Ine mfumu ndili ndi<br />
njira yogwirira mbala imeneyi. Mundipatse nthawi.<br />
Mawa nyama zonse zisabwere kuchitsime kuno.<br />
Nyama zonse zibwere mkuja, mawa zitsotse osamwa<br />
madzi. Mkuja, nyama zonse zidzapeza mbala imene<br />
ikuba madzi a mu Mzizime. Nonse mudzabwere<br />
kudzaona mbalayo.” Nyama zonse zitamva mawu a<br />
Kalulu, zinakondwera ndipo nkhawa zawo zinayamba<br />
kuchepa.<br />
Kalulu atachoka apo, anatenga nkhwangwa n’kulowa<br />
m’tchire. Atatero, anapeza mtengo ndipo anasema<br />
chifanizo cha munthu. Anatenganso phula la njuchi<br />
ndi ulimbo n’kuyamba kumata thupi lonse la chosema<br />
chija. Atatha, anachinyamula n’kupita nacho<br />
pachitsime chija. Atafika, anatenga chifanizirocho<br />
n’kuchikumbira pansi kuti chiime chilili ngati<br />
munthu.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
330
Atamaliza kuchita zimenezi, Kalulu anapita kwa<br />
bwenzi lake Nyani ndipo anamuuza kuti, “Bwenzi<br />
langa, kodi dzulo unali kuti?” Nyani anayankkha kuti,<br />
“Bwanawe, ine dzulo pamodzi ndi banja langali,<br />
tinakaba madzi kuchitsime china pafupi pomwepa. Ife<br />
satiloleza kumwa madzi kumeneko chifukwa timati<br />
tikapita, chitsime chonse timachiphwetsa. Moti<br />
anatiletsa kuti tisadzamwenso madzi pachitsimecho.”<br />
Kalulu anauza Nyani kuti, “Bwenzi langa, ine<br />
ndabwera kudzakuchenjeza. Nyama zonse zaika<br />
mlonda kuchitsime chija. Mlondayo amafa msanga<br />
akamumenya kumsana kwake. Iwe mawa upite ndi<br />
banja lako kukamwa madzi. Ukasamale kuti mlondayo<br />
asakakupenye. Ndiye ukatulukire kumbuyo kwake<br />
ndipo usakaponde masamba ouma kuti mlondayo<br />
asakamve mtswatswa wako. Ukakafika kalimbe<br />
mtima, ukalikutumule khofi n’kumenya mlondayo,<br />
ukaona kuti nthawi yomweyo akafa. Uvutikirenji ndi<br />
ludzu ngati umachita kufuna kuti uzimwa madzi<br />
ambiri, si ndi mmene unabadwira! Ukakachipanda<br />
khofi, ukachipondenso ndi mwendo mwamphamvu,<br />
ukaona kuti nthawi yomweyo chafa ndipo iwe ukamwa<br />
madzi mtima uli zii.”<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
331
Nyani atamva izi anati, “Zikomo bwenzi langa. Wachita<br />
bwino kundipangira nzeru yotereyi, nanga tife ndi<br />
ludzu chitsime chilipo?” M’mawa kwambiri Nyani<br />
pamodzi ndi banja lake analawirira kuchitsime chija.<br />
Atafika pafupi nyani anabanika nalo khofi.<br />
Anatambasula dzanja lamanja ndipo analikutumula<br />
khofi, limvekere m’mutu mwa mlonda uja kuti phwaa!<br />
Pamene nyani ankati achotse dzanja, zachosoni,<br />
linakanirira. Analiponyanso lamanzere khofi kuti<br />
phwaa! Zachisoni linakaniriranso. Tsopano<br />
anamuponda mlonda ndi miyendo yonse iwiri,<br />
zachisoni, miyendo yonse inakanirira. Tsopano nyani<br />
anayankhula, “Aaaa! Koma iwe uli ndi chipongwe eti?<br />
Bwanji ukugwira dzanja langa? Tandisiya msanga!<br />
Ndati undisiye iweee! Kodi sukumvaaaaaaa? Eeee?”<br />
Nthawi yomweyo kunamveka kulira kwa nyama,<br />
nyamazo zimabwera kuchitsimeko kudzamwa madzi!<br />
Kalulu anali m’gulu la nyamazi. Kalulu anati, “A<br />
Njovu, taonani mbala ija iyoooo! yagwidwa. Ine<br />
ndangochepa msinkhu koma taonani mmene<br />
ndagwirira kapolo wanuyooo!” Nyama zonse<br />
zinathamanga, n’kugwira wakubayo. Posakhalitsa,<br />
Njovu inaveka Kalulu ufumu ndipo inati, “Ufumu ndi<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
332
wako chifukwa cha nzeru zako!”<br />
Mafunso:<br />
1. N’chifukwa chiyani Njovu inaitanitsa<br />
msonkhano?<br />
2. Kodi anyani analakwa chiyani kuti awakanize<br />
kumwa madzi a pachitsime chija?<br />
3. Nanga n’chifukwa chiyani Kalulu anapusitsa<br />
Nyani?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
333
Phwando la Kalulu ndi Fulu<br />
Kalekalelo, Kalulu ankakonda kutchera misampha.<br />
Nthawi zambiri iye ankati akagwira nyama,<br />
ankagawirako bwenzi la pamtima Fulu. Ankachita<br />
zimenezi akamachoka kowonjola nyama zomwe<br />
zinakodwa m’misampha yake.<br />
Pa nthawiyo, Njovu ndi Mvuwu zinali paubwenzi<br />
wobwerekana nsalu. Kumene kunali Njovu, a Mvuwu<br />
ankapezekanso komweko. Kangapo konse a Ng’ona<br />
anauzapo onsewa kuti, “Koma anzanga inu, ubwenzi<br />
wotere n’ngoipa. Bwanji simumafuna kutayana? Kodi<br />
simudziwa kuti mukadzakumana ndi ngozi mudzafera<br />
pamodzi?” “Hahaha! Mwana iwe ukuti chiyani?<br />
Akuluakulu ngati ife chingationekere n’chiyani?<br />
Sukudziwa kuti ife ndife mphangala zokhazokha?”<br />
anatero Njovu poyankha a Ng’ona. “Kodi mwana iwe,<br />
aliponso wina woposa ife pa mphamvu? Sudziwa eti?”<br />
Anafunsa chotero a Mvuwu.<br />
Tsiku lina Kalulu akuyendera misampha yake, anaona<br />
mapazi a Njovu ndi Mvuwu. Mumtima mwake ali,<br />
“Agalu amenewa tsiku lina tidzaonana. Amenewa ndi<br />
amene akumaba nyama m’misampha yanga, mbala<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
334
zakuba!”<br />
Kalulu atabwerera anafika kwa Fulu ali, “Bwenzi langa<br />
pepa, lerotu udyera therere. Mbala zikungoba nyama<br />
zanga m’misampha. Ndikukhulupirira kuti ndi Njovu<br />
ndi Mvuwu, ndaonera mapazi awo. Ndikadakhala ndi<br />
chingwe cholimba ndikadawatchera msampha,<br />
ndikanawaonetsa malodza.” Fulu anati, “Bwenzi langa,<br />
khala chete, ine ndili ndi chingwe chachitali cha<br />
nsambo zopota. Dikira ndikupatse. Ife tikufuna<br />
kumadya nyama tsiku ndi tsiku ndiye sitingalole agalu<br />
amenewa aziba nyama zako ayi.”<br />
M’mawa mwake, Kalulu anatenga chingwe chija<br />
n’kupita nacho pampita wa Njovu ndi Mvuwu.<br />
Atasunzumira potero, anaona Njovu ndi Mvuwu<br />
zikubwera. Kalulu anatenga chingwecho nachinjatirira<br />
ku muzu wa mtengo waukulu umene udatemedwa<br />
ndipo nayenso anachita ngati wadzinjata.<br />
Njovu ndi Mvuwu zitafika zinati, “Oooooooo! watani<br />
mnzathu woyenda?” Kalulu ali “Heeee!<br />
Sindingakuuzeni chifukwa sindifuna kuti anthu ena<br />
akumane ndi zimene ndikukumana nazo ine pano<br />
chifukwa tingachuluke. Komabe poti tonsefe ndife a<br />
mliyenda m’tchire muno, inu nokha ndikuuzani. Koma<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
335
mulonjeze kuti simuuza wina ayi!” “Kodi ife umatiyesa<br />
ana eti? Suona mathunthuwa kodi? Tatiuza,<br />
sitikanena kwa aliyense!” anatero Njovu.<br />
Tsopano Kalulu anati, “Monga mwaonera kuti chingwe<br />
chansambo za mkuwa simunachione, chingwe<br />
chimenechi chimapatsa mphamvu, kapena kuti<br />
mangolomera. Mwakuti inu nonsenu kuyambira lero<br />
simungandichite kanthu ayi, mwachepa!” “Aaaaaaa!<br />
Ukuti chiyani?” anafunsa Mvuwu.<br />
“Kodi simukumva? Inu nonsenu pa mphamvu, osati<br />
msinkhu ayi, mwachepa ndipo ndinu makanda<br />
ang’onoang’ono osamera ndi mano omwe! Kapena<br />
ndinene kuti ndinu nthumbidwa!” anatero Kalulu.<br />
Kalulu anapitiriza kunena kuti, “Ngati mukuchita<br />
makani, mawa tiyesane. Inu awiri mugwire chingwe<br />
cha nsambochi mukhale kuseri kwa kaphiri aka, ine<br />
ndikakhala kuseri kwa Phiri ilo. Nonsenu pamodzi<br />
mukakoke chingwechi kuti muone zimene zichitike.”<br />
Njovu inati, “Ha! Ndikangokusiyira Mvuwuyu basi,<br />
akathane nawe. Mwana wakhanda ungachite chiyani<br />
ndi mapiri ngati ano? Taona, kunotu ndi kugomo osati<br />
masewera ukuchita apawa.” Anatero a Njovu<br />
podzitamandira.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
336
M’mawa kutacha, onse anakumana pa kaphiri<br />
kotchedwa Talala. Chingwe cha mkuwa chija<br />
chinayalidwa kuseri ndi kuseri kwa phirilo. Fulu<br />
patsiku limeneli anabwera kudzawonerera<br />
mpikisanowo ndiponso anasankhidwa kukhala<br />
wolamulira mpikisanowo. Kalulu anatenga chingwe<br />
chija nachinjatirira kumtengo waukulu wa mlambe.<br />
Tsopano poyamba, a Njovu anasiyira a Mvuwu okha<br />
kuti akokane ndi Kalulu.<br />
Fulu analamulira motere, “Tsopano aliyense agwire<br />
chingwe! Konzekani, kokaaaaaaa!” Zimene zinaoneka<br />
pamenepo zinali zoopsa. Mvuwu idayesa kuchita<br />
kakalakakala koma inaona kuti Kalulu ali nju! “Pepa<br />
mnzanga Njovu. Nkhondo yakula, Kalulu ujadi ali ndi<br />
mphamvu.” Anayesanso ndithu ndi mphamvu zake<br />
zonse koma Kalulu anali nju! osasunthika. Kenako<br />
Mvuwu inati, “Achimwene a Njovu, tiyeni tithandizane!<br />
Mmenemo Fulu ali, “Koka! Kokaaa!” Pamenepo n’kuti<br />
mbali imene kunali Njovu ndi Mvuwu, mitengo<br />
itawandikawandika, ina itathyokeratu, miyala<br />
inkangogubuduzikagubuduzika, fumbi lili kobooo!<br />
Nthawi imeneyi, Kalulu n’kuti atangokhala pamwala<br />
ali neng’a, akusuta fodya ali phee. A Njovu anayesetsa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
337
kukoka koma kenaka anayamba kumangodzigwera<br />
okhaokha, kenaka kumangogwerana ndi a Mvuwu,<br />
Njovu itaona kuti zavuta inati, “Aaa! Koma n’zoonadi<br />
Kalulu lero kutichititsa manyazi chotere! Mnzanga<br />
Mvuwu, tiyeko tigonje timunyengerere kuti nafenso<br />
atigawireko mphamvu zakezo!”<br />
Tsopano Njovu ndi Mvuwu anakweza manja awo<br />
m’mwamba kusonyeza kugonja. Fulu analamula,<br />
“Chingwe pansi! Yagonja Njovu ndi Mvuwu! Kalulu<br />
wapambanaaa!” Nthawi yomweyo Kalulu anamasula<br />
chingwe chija n’kuchitaya pansi. Onse tsopano<br />
anakwera pamwamba pa phiri la Talala ndipo<br />
atakumana, a Njovu anati, “Aaa! Iwe Kalulu<br />
takhulupirira zija umanenazi. Tsopano madodafe<br />
ndithu tikhale opanda mphamvu? Ayi usatero,<br />
utipatseko mphamvu zakozi!” Kalulu anati, “Tiyeni<br />
nthawi yomwe ino pamalo pompaja kuti<br />
ndikakunjateni. Inu a Njovu tinjata chitamba<br />
chanuchi. Inu a Mvuwu tikunjatani miyendo yanuyi.”<br />
Atatha kuwanjata, Kalulu anawatembenukira<br />
amvekere: “Mwafa lero mafana! Mwafa lero! Mbala inu<br />
mwakhala mukundibera nyama zanga!” Njovu inati,<br />
“Hiii! Tikufa!” Mvuwunso ili, “Mayooo! Tikufa!” Ndiyetu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
338
panali matatalazi. Tsoka ilonso anali atatopa kale<br />
chifukwa cha mpikisano uja. Ndiyetu a Njovu<br />
amvekere khuu! kugwa, nawonso a Mvuwu, khuu!<br />
Kugwa chagada!<br />
Nthawi yomweyo Kalulu anathamanga kukasokolotsa<br />
ana ake amene anawabisa, mpeni uli kumanja ali,<br />
“Lero kuli chiphwando cha nyama yokhayokha.” Fulu<br />
naye ali, “Ine ndiyambira kuchekako Njovuyi. Lero kuli<br />
chiphwando chosasunsa.” Kalulu ndi ana ake pamodzi<br />
ndi Fulu anapanga chiphwando chadzaoneni ndipo<br />
anadya a Njovu ndi a Mvuwu.<br />
Mafunso<br />
1. Kodi ndi ndani ankaba nyama za Kalulu?<br />
2. Kodi chingwe cha mkuwa chinapatsadi<br />
mphamvu Kalulu?<br />
3. N’chifukwa chiyani Njovu ndi Mvuwu<br />
zinagonja?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
339
Chimene Kalulu Amagonera Diso Lili<br />
Tong’o!<br />
Tsiku lina Kalulu akuongola miyendo m’malunje<br />
anamva phokoso la nyama zomwe zinkaoneka kuti<br />
zinali pa chimsonkhano m’nkhalango yotchedwa<br />
Thuma. Pamene Kalulu anaima, anamva dzina lake<br />
likutamulidwa. Iye anadabwa popeza sanalandire<br />
mthenga wa msonkhano wotere. Kenaka anamva<br />
mawu onena za kuuma kwa mitengo ndi udzu. Chaka<br />
chimenecho mvula inapenga moti kunja kudali gwa<br />
chifukwa cha chilala. Udzu, mitengo komanso zomera<br />
zonse zinaumiratu. Chakudya cha nyama zonse<br />
chinkasowa moti m’masiku amenewo nyama<br />
zinkangodya dothi la mdambo. Nyamazi zinkatchula<br />
malo angati amenewa kuti Phukuto.<br />
Kalulu anayamba kupenekera kuti cholinga cha<br />
msonkhanowo chinali kukambirana za njala imene<br />
inali m’kamwam’kamwa. Kalulu anasendera pafupi<br />
ndithu ndipo anadabwa atangoona nyama<br />
zowerengeka zokha, popeza zinali pobisalika. Mawu a<br />
Njovu anali kumveka kuti, “Anzanga nonse mwabwera<br />
pano, njala ndimeneyi. Njala yopanda pothawira yotere<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
340
timaitcha chinkukuluzi. Koma ife bwanji kamwana<br />
kaja kamati ndi mfumuka palibe? Ka Kalulu<br />
kameneka ine ndimati ufumu wake uthe lero. Bwanji<br />
sabwera pamavuto ngati awa? Ine ndinam’tumira<br />
mthenga, koma onani sanabwere. N’chifukwa chaketu<br />
ine ndikuti ufumu wake watha lero! Nanga inu<br />
mukuganiza bwanji?” “Indeee! Tiyeni tipungure ufumu<br />
wakewo kuti aone polekera,” nyama zonse zinatero<br />
mwa mabvume.<br />
Zonse ankanena Njovu zoti adatuma mthenga kwa<br />
Kalulu, linali bodza lofuka utsi. Njovu inachita izi<br />
potengera chidani chakale. Inachita dala kuti Kalulu<br />
atsike pampando. Kenako kunatulukira chimoto<br />
chimene anthu a liwamba anatentha, ndipo Kalulu<br />
ataona motowo zinamuvuta popeza motowo<br />
unkalunjika pamene iye anabisala.<br />
Kalulu nzeru zinamuthera popeza amafuna kumva<br />
zonse zimene ankambirana makamaka zothetsa<br />
ufumu wake wa zaka zambiri m’nkhalangomo. Kalulu<br />
anangothawira kunyumba kwake kuti akayambe<br />
wapeza nzeru zina.<br />
Mmawa kutacha Kalulu anatuma mthenga kwa<br />
bwenzi lake Nyani, kuti awonjezere nzeru chifukwa<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
341
mumtima adati, “Nzeru umati n’za mnzako si za<br />
wekha. Mutu umodzi susenza tsindwi. Safunsa adadya<br />
phula. Nzeru zayekha adaviika nsima padziwe. Nyama<br />
ya liuma inafa ndi ludzu. Dombolo n’kuwombolana.<br />
Ndiye ine ndiyenera kufunsira nzeru kwa bwenzi<br />
langa.”<br />
Nyani asanafike, Kalulu anaika mphika pamoto<br />
kuphika zikhawo zosakaniza ndi bowa, chifukwa<br />
mkazi ake anali akudwala. “Odii! Odii kumeneko!”<br />
Mawu anamveka. “Lowani,” anatero Kalulu. “Oooo!<br />
Kodi ndi bwenzi langa Nyani! Khala pachitsapa.<br />
Pepatu wandipeza ndikuphika. Alamu ako sakupeza<br />
bwino ayi. Chibayo chidangowati thi! Moti ali<br />
dathidathi! Ndiye n’chifukwa chaketu wandipeza<br />
ndikuphika,” anatero Kalulu. “Pepa mbale wanga!”<br />
anayankha motero Nyani.<br />
“Ndakuitana ndine bwenzi langa,” anayamba nkhani<br />
motero Kalulu. “Kodi kumsonkhano dzulo lija kunali<br />
zotani? Ine sadanditumire mthenga wondidziwitsa.”<br />
“Ehe! Kodi waiwala, pajatu ife awiri ndife odedwa,<br />
inenso sadandiitane. Ndidangomva akuti a Njovu<br />
akuchotserani ufumu. Koma usade nkhawa mawa<br />
ndibwera ndi mankhwala. Malo ako ano<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
342
ndidzakonzakonza moti mitengo yonseyi ikhala ya<br />
biriwiri! Udzu onse wawumawu ukhalanso uli<br />
biriwiriwiri! Nyama zonse, zidzakukhumbira kwambiri<br />
n’chifukwa chake nditadzaikemo chinjoka kuti<br />
chizidzaluma nyama zakuba n’kufera pomwepo. Mbali<br />
iyo, ndi mankhwala omwewo, tibowola kasupe wa<br />
madzi ozizira bwino.”<br />
Atamaliza kudya chakudya chawo, Nyani anatsanzika<br />
n’kunyamuka kumapita kwawo. M’mawa kutacha<br />
Nyani anabwera ndi mankhwala ake amene<br />
anawatchula dzina loti Nkhonkha. Atachita<br />
mankhwala aja, panatuluka chinsipu chobiriwira,<br />
mitengo ya zipatso, ndipo madzi anabowoledwa moti<br />
ankangoti popopo!<br />
Mbiri ya mudzi wa Kalulu inamveka ndipo nyama<br />
zambiri zinkabwera kudzaona zodabwitsa ndi<br />
zachilendozo.<br />
Njati: Odii a Kalulu! Tadzaona zozizwitsazi! Zatheka<br />
bwanji?<br />
Kalulu: Ngakhale munathetsa ufumu wanga, koma<br />
mukufa ndi njala!<br />
Njati: Ngati ndine! Ee! Ndi a Njovutu omwe<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
343
mukulimbirana nawo ufumuwo!<br />
Mbidzi: Pepa Kalulu ndimwe nawo madzi ndingafe ndi<br />
ludzu!<br />
Nyama zonse zimene zidakaona mudzi wa Kalulu<br />
zinayamba kunyoza mawu amene ananena a Njovu oti<br />
Kalulu ufumu uthe. Njovu atamva zimenezi anachita<br />
manyazi popeza sankalandiranso ngakhale moni kwa<br />
nyama iliyonse.<br />
Nyama zonse tsopano zinaona kuti Kalulu ngakhale<br />
ufumu unamuchokera, koma anali wosangalala<br />
popeza anali kumwa ndi kudya bwino. Mkango ndi<br />
Mvuwu onse anapangana kuti aitanitse msonkhano.<br />
Nyama zonse pamodzi ndi Njovu zinabwera<br />
kudzakambirana za mavuto awo. Potsiriza anaganiza<br />
kuti onse apite kwa Kalulu kukapepesa ndi kufunsira<br />
nzeru kuti dziko libwerere msipu wosilirika ndi<br />
mitengo yobiriwira pamodzi ndi madzi.<br />
Atafika kwa Kalulu, nyama zonse zinanena mavuto<br />
awo mwatsatanetsatane.<br />
Mkango: Bwana Kalulu, ife tabwera kuti<br />
tidzakupepeseni. Tinakulakwirani zedi. Chimunthu<br />
china chachikulu khutu, chidatilakwitsa. Inu ufumu<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
344
wanu udalipoooo!<br />
Nyama zonse: Eeee! Indediii! Zoonaaa!<br />
Mkango: Bwana Kalulu, ife ana anu tikomereni mtima<br />
potikonzera nkhalango yathuyi. Taonani madzi<br />
mulibe, msipu mulibe komanso mitengo yayiwisi<br />
mulibe.<br />
Kalulu: Dzikoli silikonzeka! Ngati mukufuna kuti<br />
likonzeke aliyense akaphe amake. Kenako mubwere<br />
kuno mukabwere ndi mitu yawo kuti tidzakonzere<br />
mankhwala! Zamvekaa?<br />
Nyama zonse: Indeeeee! Mawa ife tibwera nayo<br />
mituyo!<br />
Kalulu: Ine kuti ndipeze mukuzionazi ndinayamba<br />
ndapha mayi anga, n’chifukwa chake lero ndili<br />
pabwino!<br />
Nyama zonse zinabalalika kukapha amayi awo<br />
n’kuwadula mitu. Mitu ija isadabwere, Kalulu<br />
ananyamula mayi ake usiku n’kukawabisa mumtengo<br />
mbali ina ya tchire m’nkhalango ya Thuma.<br />
Tsopano m’mawa kutacha, nyama zonse zinabwera<br />
ndi mitu ija. Kalulu anaunjika mituyo n’kuika nkhuni<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
345
pamwamba pake ndipo anaitentha mpaka inasanduka<br />
phulusa lokhalokha. Kenako Kalulu anati, “Eyaaa!<br />
Ntchito yanga ndayamba tsopano, pitani kwanu.<br />
Mukhoza kumwa nawo madzi angawa, mukhozanso<br />
kudya msipuwu ndi chilichonse chimene mungakonde<br />
musanapite kwanu!” Nyama zija zinayamba<br />
kulimbirana makamaka zikhawo za dinde, chinkhwisi,<br />
ndekera, nthochi ndi zina zotero.”<br />
Patapita masiku atatu nyama zija zinabweranso<br />
kudzafunsa ngati panali mwayi uja adalonjeza Kalulu.<br />
Kalulu anangowauza kuti phulusa la mitu lija<br />
likugwira ntchito. Anawauzanso kuti, “Tsopano dzikoli<br />
lili pafupi kukonzeka. Koma phulusa la mitu ija<br />
lachepa. Mvula ndi madzi ndimakapempha kwa Azimu<br />
a m’nkhalango ino, ndiwo amene afuna phulusa lina,<br />
lijali lachepa. Tsopano Azimuwo akufuna phulusa lina<br />
la mitu ya atate anu. Motero katengeni mitu ya atate<br />
anu kuti tidzasakanize pamodzi. Zikatero posachedwa<br />
mudzalandira zonse. Dziko lino la Thuma<br />
sikudzakhalanso mavuto ngati amenewa.”<br />
Nyama zonse zinapita n’kukapha atate awo<br />
n’kubweretsa mitu yonse kwa Kalulu. Kalulu anaotcha<br />
mitu ija n’kutenga phulusa. Nyama zija zinapita<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
346
Kalulu ananyamula atate ake n’kukawabisa kumalo<br />
kuja anabisa mayi ake. Pamene amachoka kumeneko,<br />
nyama zina zinamuona ndipo zinadodoma popeza<br />
anatenga nsengwa zodyera chakudya.<br />
Kenaka patatha sabata, nyama zonse zija<br />
zinabweranso kwa Kalulu. Kalulu anati, “Zoona<br />
anzanga muli m’mavuto, koma ndinapita kuphanga<br />
kumene kukhala Azimu. Phulusa lija ndinapereka<br />
koma Azimuwo akuti phulusa lija lachepa m’pofunika<br />
kuwonjezera lina la ana anu oyamba, achisamba.<br />
Mukatero sabata lamawa mulandira mvula ndi zonse<br />
zimene mukufuna.”<br />
Nyama zija zitamva mawu amenewa zinayamba<br />
kukhumudwa mumtima, zambiri zinayamba<br />
kung’ung’udza zimvekere, “Anzathu, izitu tipwetekeka<br />
nazo. Kodi tikathanso mtundu umene madziwo<br />
tidzamwa ndi ndani? Taonani umo taphera anthumu!<br />
Zabodza, Kalulu akufuna tithane tokha. Kodi<br />
simunamudziwebe Kalulu? Akhozatu kukhala<br />
akuponya nkhondo ndi ife mobisalira ife osadziwa.<br />
Tiyeni tichenjere!”<br />
Mmawa, nyama zonse zinabwera ndi mitu ya ana awo<br />
achisamba. Kalulu anatenga mitu ija n’kuiotcha ndipo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
347
anatenga phulusa lija. Patapita masiku awiri, nyama<br />
zonse zinabwera. Kalulu anati, “Ine ndabwera<br />
posachedwa kwa Azimu kuja. Phulusa lija ndapereka,<br />
koma akuti pakufunika kuwonjezeranso lina kuti<br />
tsopano likwane bwino n’cholinga choti mvula ibwere<br />
yoopsa, yamkokomo wa madzi. Motero mawa mubwere<br />
ndi mitu ya zitsitsa misepa zanu. Mufulumire!”<br />
Nyama zonse tsopano zinadodoma, zina zinakwiya<br />
koopsa. Fulu, Nkhandwe ndi Fisi anasankhidwa kuti<br />
akhale maso a nyama zonse. Udindo umene anali<br />
nawo ndi kubisalira Kalulu kuti aone mayendedwe ake<br />
chifukwa zochita za Kalulu zinayamba kuwatayitsa<br />
mtima.<br />
Nyama zonse zikupita kwawo, Kalulu analowa<br />
m’nyumba natulukamo ndi phukusi la masamba a<br />
mtengo wa msuku. Waliutsa liwiro kulowera kutchire.<br />
Fisi, Nkhandwe ndi Fulu, analiutsanso lawo liwiro<br />
kumutsatira. Atakweza maso, anaona Kalulu wagwira<br />
chingwe ali kukwera mumtengo, Fulu anati, “Anzanga<br />
mukuona zimene Kalulu akuchita?”<br />
Fisi: Kodi Kaluluyu ndizo amachita?<br />
Nkhandwe: Kodi n’kukhala chiyani chimenechi?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
348
Fulu: Bwino wosakweza mawu angatimve.<br />
Pamene Kalulu anafika patsinde la mtengo, anayamba<br />
kuimba kanyimbo namati, “Mayi! Mayi! Tayire<br />
kachingwe! Mayi! Mayi! Tayire kachingwe!”<br />
Tsopono anangoona chingwe kuchokera m’mwamba<br />
kuti sololokuu! Pansi khwa! Kalulu gwi! Lendee!<br />
kukwera mumtengo. Kalulu atatsika anapita<br />
kunyumba. Fisi anapita patsinde la mtengo uja<br />
nayambanso kuyimba, “Mayi! Mayi! Tayire kachingwe!<br />
Mayi! Mayi! Tayire kachingwe!”<br />
Posakhalitsa anaona chingwe chija kuti, sololokuu!<br />
Pansi chimvekere khwa! Fisi gwi! Lendee! mpaka<br />
anakafika m’mwamba muja kalakatu! Pamene amayi<br />
ndi atate a Kalulu anaona chilombo Fisi, analira,<br />
“Mayo! Mayoo!” Fisi ali “Mwafa lero! Mwafa lero!”<br />
Zitatero, Fisi ndi Nkhandwe anadula mitu ya awiriwa<br />
ndipo anatsika n’kupita kumene kunali nyama zina<br />
zija.<br />
Atafika Fisi anati, “Anzathu, tachita ntchito imene<br />
munatipatsa. Onani mitu iwiri iyi. Kalulu anabisa<br />
amake ndi atate ake kutchire m’mwamba. Ife<br />
tinamulondola, n’kubisala. Posakhalitsa tinaona<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
349
chingwe chili kuchoka m’mwamba. Iye atagwira<br />
chingwecho taona wakwera m’mwamba muja. Atatsika<br />
ifenso tinayimba kanyimbo kakeko ndipo tinangoona<br />
chatsika chingwe, ifenso pogwira, taona takwera<br />
m’mwamba muja. Poti tione, taona ndi amake ndi<br />
atate a Kalulu. Atationa basitu kuyambapo kulira. Ife<br />
ii basi, takong’ontha onse!” Nyama zonse zitamva<br />
zimenezi zinati, “Mwagwira ntchitooooooooooo!<br />
Mwagwira ntchitoo!”<br />
Kalulu atamva za nkhaniyi anathawa n’kukamanga<br />
malo atsopano pachitsamba. Kufikira lero amagona<br />
pachitsamba pomwepo maso ali tuzuuu kuopa<br />
milandu imene anapalamula pouza anthu kuti<br />
akufuna mitu yoti apetulire mvula.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
350
Mafunso<br />
1. N’chifukwa chiyani Njovu inaganiza zothetsa<br />
ufumu wa Kalulu?<br />
2. Kodi Kalulu anamva bwanji za nkhaniyi?<br />
3. Kodi mukuganiza kuti Kalulu ankanena zoona<br />
pamene anauza anzakewo kuti akufuna mitu<br />
n’cholinga choti awabweretsere mvula?<br />
4. N’chifukwa chiyani Kalulu amagona diso lili<br />
tuzu?<br />
5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
351
Mfumu ndi Nyemba Zophika<br />
Kalelo kunali mfumu ina yokalamba kwambiri.<br />
Mfumuyi inali ndi nkhawa kwambiri chifukwa inalibe<br />
mwana woti n’kulowa ufumu wake. Ndiye itaona kuti<br />
chaka chimenecho sigonera, inaganiza zosankha<br />
mwana m’modzi wa mu ufumu wake kuti akhale<br />
mwana wake wodzalowa ufumuwo. Atafufuza m’dziko<br />
lonse anapeza anyamata khumi omwe ankaoneka<br />
okongola komanso a khalidwe labwino. Koma popeza<br />
inkafuna mwana m’modzi yekha inawauza kuti,<br />
“Tsopano chatsala chinthu chimodzi choti muchite<br />
kuti ndipeze mnyamata amene atakhale mwana<br />
wanga.” Kenako anapereka kwa mnyamata aliyense<br />
nyemba imodziimodzi n’kuwauza kuti akaidzale<br />
kunyumba kwawo n’kuisamalira kwa milingu itatu.<br />
Mwana amene adzasamalire bwino mbewu yake<br />
adzatengedwa kukhala mwana wa mfumu!<br />
Anyamatawo atangomva zimenezi analiyatsa liwiro, wa<br />
kwawo kukadzala mbewu yawo. Koma mnyamata wina<br />
anadabwa kwambiri ataona kuti mbewu yake<br />
sikumera. Mnyamatayo anachita chilichonse kuti<br />
imere, koma palibe chinachitika. Anzake aja<br />
anayamba kumuuza kuti akangogula ina n’kuidzala<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
352
chifukwa akapanda kutero zimuvuta. Koma makolo a<br />
mwanayo anali oopa Mulungu moti anamuuza kuti<br />
asachite zimenezo.<br />
Kenako tsiku linafika loti apite kwa amfumu aja. Ana<br />
asanu ndi anayi anapezeka kuti mbewu zawo<br />
zinamera. Mfumuyo inayamba kufunsa<br />
m’modzim’modzi kuti, “Kodi mbewu zimene<br />
ndinakupatsani zinamera?” ndipo anyamata onse<br />
anayankha kuti “Inde mfumu yanga.” Kenako<br />
mfumuyo inagwedezera mutu n’kupitanso kwa wina<br />
mpaka inafika pa mnyamata yemwe nyemba yake<br />
sinamere uja. Mnyamatayo ankangonjenjemera ndi<br />
mantha. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi unaitani<br />
nyemba imene ndinakupatsa kuti ukadzale?” Iye<br />
anati, “Ndinaidzala n’kumaisamalira koma sinamere.”<br />
Mfumuyo inagwira mkono wa mnyamatayo n’kupita<br />
naye pamene panali mpando wachifumu n’kunena<br />
kuti, “Nonse ndinakupatsani nyemba zophika, ndiye<br />
zatheka bwanji kuti za enanu zimere? Nanga nyemba<br />
zophika zingamere ngati? Munthu amene ndimafuna<br />
kuti akhale mwana wanga komanso adzakhale mfumu<br />
ndimafuna akhale ndi khalidwe limeneli la kuona<br />
mtima ndipo ndi mwana uyu yekha amene wachita<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
353
wino. Enanu zipitani!”<br />
Mafunso:<br />
1. Kodi n’chifukwa chiyani nyemba ya mwana<br />
wina sinamere?<br />
2. Kodi mukuganiza kuti nyemba zimene<br />
anyamata ena asanu ndi anayi aja anadzala zinali<br />
zimene anapatsidwa ndi mfumu ija?<br />
3. N’chifukwa chiyani mwana amene mbewu yake<br />
sinamere uja anasankhidwa kukhala mwana wa<br />
amfumu?<br />
4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
354
Angongole<br />
Mayi: Kukabwera angongole aja, uwauze kuti<br />
ndachokapo.<br />
Nyamazawo: Ndiwauze kuti mwapita kuti?<br />
Mayi: Kwa Chinsapo.<br />
Kenako angongole anatulukira ndipo anayamba<br />
kuodira.<br />
Angongole: Odiiiiii. Odi kumenekooo!<br />
Nyamazawo: Eeeee.<br />
Angongole: Mayi ako ali kuti?<br />
Nyamazawo: Achokapo, apita kwa Chinsapo.<br />
Angongole: Abwerako nthawi yanji?<br />
Nyamazawo: Aaaa, dikikirani kaye ndikawafunse.<br />
Angongole: Ukawafunsa bwanji, mmesa wati apita<br />
kwa chinsapo?<br />
Nyamazawo: Ayi, ali m’nyumbamu.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
355
Fisi Anakana Mtsatsi<br />
Mlenje wina anathedwa nzeru ndi chilombo chimene<br />
chinkabwera pakhomo pake n’kumagwira ziweto zake<br />
usiku. Tsiku lina anaganiza zotchera msampha ndipo<br />
usiku umenewo anagona khutu lili panja kuti akamva<br />
chinachake adzuke.<br />
Usikuwo anayamba kumva phokoso. Asuzumire,<br />
anangoona kuti ndi fisi wakodwa pamsampha. Fisiyo<br />
ankayesayesa kuti achokepo. Mlenjeyo ataona izi<br />
anayamba kukuwa amvekere, “Fisi kunoooooooooo!<br />
Bwerani mudzandithandize kuli fisi kunoooooooo!”<br />
Anthu a m’nyumba zoyandikira anatulukadi ndipo<br />
anagwira fisiyo n’kumukwidzinga ndi zingwe. Kenako<br />
anayamba kumuimba mlandu.<br />
Munthu wina anati, “Nkhosa zanga zakhala zikusowa,<br />
ayenera ndi fisi yemweyu amene amandibera.”<br />
Winanso anati, “Ife ndiye mbuzi zathu wamaliza zonse<br />
kudya.”<br />
Panabweranso mayi wina ndipo anati, “Nkhuku zathu<br />
zonse wamaliza kukhwasula ameneyu!”<br />
Ndiyeno nkhalamba ina inati, “Nanenso dzulo<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
356
ndinayanika mtsatsi zanga pathandala, ayenera wadya<br />
ndi yemweyu chifukwa zawowa.”<br />
Fisiyo atamva mawu amenewa anati, “Agogo inuyo<br />
ndiye mukunama, bola zimene anena anzanu zija.<br />
Koma za mtsatsizi ndiye ndakukanirani. Inetu<br />
sindidya mtsatsi.”<br />
Phunziro: Fisi angakhale munthu amene akuimbidwa<br />
mlandu. Ngakhale munthu atakhale woipa kwambiri, si<br />
bwino kumangomunamizira zimene sanachite.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
357
Mlenje ndi Mkango<br />
Tsiku lina mlenje wina anapita kutchire kukasaka<br />
nyama ndi agalu ake. Atafika malo ena, agalu akewo<br />
anasokolotsa Sakhwi n’kumugwira, koma mlenjeyo<br />
anawaletsa agaluwo kuti amusiye ndipo Sakhwiyo<br />
anathawa n’kukabisala kuphanga.<br />
Kenako mlenjeyo anapitirizabe kusaka ndipo anafika<br />
pafupi ndi dziwe lina. Pamalowo panali ntchefu moti<br />
agalu ake aja anagwira imodzi n’kuipha. Pamenepo<br />
mlenjeyo anasangalala zedi podziwa kuti tsiku<br />
limenelo akadyera nyama. Koma kenako kunayamba<br />
chimvula choopsa moti mphenzi sizinkati zaomba pati.<br />
Ataona zimenezi anaganiza zolowa m’phanga lina<br />
ndipo atangolowamo anapezamo ana a mkango. Koma<br />
popeza kunali mvula yoopsa, sakanachitira mwina<br />
koma kulowabe m’phangalo. Atangolowa, mkango<br />
ujanso nawo unatulukira. Nawonso unasokoloka<br />
m’tchire chifukwa cha mvulayo. Utafika pakhomo pa<br />
phanga lake unazindikira kuti m’phanga lakelo<br />
mwalowa munthu ndi agalu ake. Mkangowo sunafikire<br />
kulowamo chifukwa unkafuna kuti uonetsetse<br />
bwinobwino ngati mlenjeyo analidi yekha mphangalo.<br />
Kenako unafunsa munthuyo kuti, “Kodi ndiwe ndani<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
358
ukupezeka m’phanga langa?”<br />
Munthuyo anayankha mwamatha zedi kuti, “Ndine<br />
munthu mfumu yanga.”<br />
Kenako Mkangowo unati, “Ndiye popeza ndakupeza<br />
m’phanga langa, utenge ntchefu waphayo uwapatse<br />
agalu akowo kuti adye. Kenako iweyo udye agaluwo.<br />
Ineyo ndidya iweyo!”<br />
Munthuyo atamva izi anachita mantha zedi moti<br />
anayamba kunjenjemera komanso kudzikodzera.<br />
Koma mlenjeyo sanadziwe kuti Sakhwi<br />
anamupulumutsa uja anabisala momwemo.<br />
Sakhwiyo anauza mlenjeyo kuti, “N’chifukwa chiyani<br />
mukuchita mantha? Mkangowutu wanena kuti<br />
mutenge ntchefuyi mupatse agaluwa adye, kenako<br />
inuyo mudye agaluwo, ndipo Mkangowo udya inuyo.<br />
Pamapeto pake, ineyo ndidya Mkango ndi ana akewa.”<br />
Mkangowo utangomva zimenezo unachita mantha<br />
kwambiri moti unathawa.<br />
Phunziro: Ndi bwino kumathandiza ena chifukwa<br />
nawenso zikadzakuvuta akhoza kudzakuthandiza.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
359
<strong>Bonwell</strong> <strong>Rodgers</strong><br />
M’bukuli muli nthano za ana. Nthano zina ndi<br />
zoti zinalembedwa ndi akatswiri akale kwambiri<br />
ndipo zinamasuliridwa n’kukonzedwa mwina<br />
ndi mwina, pomwe zina ndi za kwathu konkuno<br />
ku Malawi. Nthanozi ndi zazifupi koma<br />
zosangalatsa.<br />
<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />
360<br />
This book is dedicated to my<br />
beloved brother, Brian. I love<br />
you little brother and am<br />
always <strong>by</strong> your side.<br />
If I could save time in a<br />
bottle, the first thing that I’d<br />
like to do is to save every day<br />
till eternity passes away, just<br />
to spend them with you.<br />
If I could make days last<br />
forever, if words could make<br />
wishes come true, I’d save<br />
every day like a treasure and<br />
then again, I would spend<br />
them with you—Jim Croce.