Mpandamachokero Anthology by Bonwell Rodgers

10.03.2017 Views

MPANDAMACHOKERO ANTHOLOGY By Bonwell Rodgers

MPANDAMACHOKERO<br />

ANTHOLOGY<br />

By <strong>Bonwell</strong> <strong>Rodgers</strong>


Mawu Oyamba<br />

M’bukuli muli nthano za ana. Nthano zina ndi zoti<br />

zinalembedwa ndi akatswiri akale kwambiri ndipo<br />

zinamasuliridwa n’kukonzedwa mwina ndi mwina,<br />

pomwe zina ndi za kwathu konkuno ku Malawi.<br />

Nthanozi ndi zazifupi koma zosangalatsa. Wolemba<br />

bukuli anaona kuti anthu ambiri sakonda kuwerenga<br />

nkhani zazitali. Choncho analemba nthano zazifupi<br />

koma zomveka bwino. Nthanozi ndi zoti zikhoza<br />

kugwiritsidwa ntchito pophunzitsa kusukulu,<br />

powerengera ana komanso pocheza. Bukuli<br />

lingathandizenso ana kuphunzira ukadaulo wopinda<br />

komanso kuseweretsa mawu m’Chichewa.<br />

Kuwonjezera apo, nthano zake ndi zokhathamira ndi<br />

nsinjiro za chiyankhulo.<br />

The Series of <strong>Rodgers</strong> Bounty Books [RBB]<br />

Copyright © January 2015 <strong>by</strong> <strong>Bonwell</strong> <strong>Rodgers</strong>.<br />

All rights reserved. No part of this publication may be reproduced or transmitted in any form or <strong>by</strong> any means, electronical or<br />

mechanical, including photocopy, recording or any imformation storage and retrieval system, without permission in writing from the<br />

owner.<br />

Requests for permission should be mailed to: <strong>Bonwell</strong>rodgers91@gmail.com<br />

Phone: 0881813953, 0881831435<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

1


Nthano Zokhala ndi Maphunziro<br />

“Tikhoza kuphunzira zambiri ngakhale kuchokera kwa<br />

nyama zakutchire. Chilichonse chili ndi pokomera,<br />

kungoti umafunika kufufuza mosamala kuti upaone<br />

pokomerapo.”<br />

—Anatero Lewis Carrol m’buku lake lakuti, Alice’s<br />

Adventures in Wonderland<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

2


Mbalame Yodzimva<br />

M’nkhalango ina munali mbalame yokongola kwambiri<br />

yomwe inkadya moto chifukwa cha kuyerekedwa<br />

kwake. Dzina la mbalameyi linali Pikoko. Mbalameyi<br />

inali yaphunzo chifukwa inkanyoza zinzake zomwe<br />

zinali ndi nthenga zosaonetsa kugulu la anthu.<br />

Inalinso yodzimva komanso yodzikuza zedi. Tsiku lina<br />

mbalame zonse zitakhuta, zinapita pachitsime pomwe<br />

zinkakamwa madzi. Mbalamezi zinkafunika kufola<br />

pamzere kuti zikamwe madziwo. Ndiye chifukwa<br />

chodziona kukongola, mbalame ija yotchedwa Pikoko<br />

inangoyenda kupita kutsogolo n’kudutsa zinzake<br />

zonse zomwe zinafika mofulumira. Mbalameyi<br />

inkayenda monyang’wa ngati sipita kuchumbudzi, ili<br />

palasu palasu palasu mpaka inakafika kutsogolo<br />

kwenikweni. Anzake anaifunsa amvekere: “Chikatere?”<br />

A Pikoko pomva izi anayamba kulavula mwano.<br />

“Mulungutu enafe anatikondera! Kodi mumatichitira<br />

nsanje eti?”<br />

Mbalame zinzake zinadandaula kuti: “Chitsime<br />

n’chimodzi m’mudzi muno, aliyense ayenera<br />

kuchitiridwa mofanana kaya ali ndi nthenga zokongola<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

3


kapena ayi, chilungamo chiziyenda ngati madzi!”<br />

Koma mbalame ija inatuzula maso kwinaku<br />

ikutokosera m’mano ndipo kenako inageyanso<br />

chipongwe china cholama.<br />

“Kodi mbalame zosasamba zikudzatani kuno? . . . Inu<br />

a Khwangwala, ngati mumafuna kuchitiridwa zinthu<br />

mofanana ndi enafe ingopitani kumanda! Ndipo<br />

ndimadabwa kuti n’chifukwa chiyani nawonso manda<br />

samaona kuti enafe tili ndi nthenga zokongola?<br />

Tikazitambasula anthu amagwetsa zibwano zawo,<br />

kudabwa kumeneko!”<br />

Nang’omba atamva izi anatsutsa Pikoko. Kumenekotu<br />

ndi kuyankhula kwa ntudzu komanso kogudukira.<br />

Kukongoladi kwa mbalame n’kulinga utaiona<br />

itatsegula pakamwa! Ndikuuzeni pano mosapsatira<br />

mawu achikulire, kukongola kwa nthengaku<br />

sikungakupangitseni kukhala wanzeru! Enafe<br />

tinangoipa maonekedwewa, muntimamu si khalidwe<br />

lake. Komanso tili ndi chikondi chopangitsa munthu<br />

kuiwala kwawo!”<br />

Mbalame zina zonse zinagwedezera mitu<br />

povomerezana ndi a Nang’omba.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

4


“Mwayankhula bwino pamenepo a Nangomba!” Inatero<br />

Nthiwatiwa. A Nthiwatiwa sanadziwe kuti zimene<br />

anachitazo kunali kudzipalasira makala a moto,<br />

ukadziotche weniweni. Pa nthawiyi n’kuti Pikoko<br />

atapsa mtima, ukali ukutulukira mumphuno komanso<br />

m’makutu, kwinaku atafutukura mapiko ake pofuna<br />

kuwaonetsa anzakewo apo panagona kukongola<br />

kwake. Kenako inakoka mtsonyo ikuyangana a<br />

Nang’omba omwe anayandikana ndi a Nthiwatiwa.<br />

Ndiyeno inayamba kulavula chichewa chitalichitali<br />

chothiga ndi phunzo.<br />

“Inu a Nang’omba ndinu chibenga. Nanunso a<br />

Nthiwatiwa muli tiwa ngati nsungwi, zovala<br />

zinakuthawani kalekale. Kodi simunamve kuti<br />

munthu ukamafuna dzino lalikulu umafunika<br />

kuutumba mulomo waukulu woti uvindikirire dzinolo?<br />

Kutalika muli thobo, n’kumalephera kupeza zovala za<br />

msinkhu wanu. Mumabwerekana zovala ndi mwana<br />

wanu kapena? Mbalame zosasambanu mumatha<br />

mawu kwabasi. Kaya n’kusowa khobili logulira<br />

chinkhupule! Miyendo imeneyo ingapulumuke<br />

mutakumana ndi khwekhwe kapena chimvwapula?<br />

Mukamayenda mumangonunkha nkhwema<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

5


kunkhwapa, simutisanzitsa inu? Kapena mumafuna<br />

enafe tizichita nseru kuti chakudya m’malunjemu<br />

chizitibwerera kukhosi! Umbombo wamtundu wanji<br />

wofuna muzigalika nokha! Mukamayenda muli mimba<br />

tiyetiye, nthenga zili yaviyavi, n’kumangooneka ngati<br />

kamvuluvulu . . .”<br />

Chipongwe chimenechi chinawafikapo a Nthiwatiwa<br />

moti anayamba kuphulusika. Kenako anati:<br />

“N’chifukwa chiyani anthu omwe muli pabwino<br />

mumayankhula motumbwa?”<br />

Koma a Pikoko anati: “Pajatu chilungamo<br />

n’chipongwe! Kungoti enafe sitibisa mawu. Ena<br />

akamatizolowera timangowamasura!”<br />

Ndiyeno a Mkuta analowererapo n’kuuza a Pikoko<br />

kuti, “Nafenso tikumasureni lero. Khalidwe lanu<br />

limatinyansa, bolanso chimbudzi cha njovu kapena<br />

fungo la dzila lowola.”<br />

“Choka wouma mutu iwe!” Anatero a Pikoko.<br />

“Namalenga ndiye anandinikha kukongolaku. Ngati<br />

mumadziimba mlandu chifukwa cha kusaoneka bwino<br />

kwanuko, mukawasumire makolo anu! Kodi<br />

ndikanena chilungamo ndiye ndisanduke woipa?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

6


Osavula zigoba mwavalazo bwanji?”<br />

Mbalame zonse zinadzuma ndipo ina yomwe inkamwa<br />

madzi inatsamwa. Nthawi yomweyo Kadzidzi yemwe<br />

n’kuti maso ake ali psuu chifukwa chosala tulo, zikope<br />

zili thyo kuthyoka, anati: “A Pikokoo, palibetu<br />

wangwiro padziko lapansi pano. Taonani miyendo<br />

yanuyo!”<br />

Mbalame zonse zinafa nawo nseko ndipo zina<br />

zinangotsala pang’ono kukomoka chifukwa cha<br />

chikhakhali. Zinkaseka miyendo ya a Pikoko yomwe<br />

inali mbuu kutuwa ndipo inkangooneka ngati<br />

zotokosera m’mano. Chifukwa cha manyazi, a Pikoko<br />

anangosamukapo pachitsimepo, koma nyota<br />

itangalula kukhosi.<br />

Phunziro: Si bwino kukhala wodzikuza chifukwa<br />

ngakhale utakhala ndi luso umakhala ndi penapake<br />

pamene umalephera.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

7


Mafunso:<br />

1. N’chifukwa chiyani a Pikoko samafuna kukhala<br />

pamzere?<br />

2. Kodi n’chiyani chikusonyeza kuti a Pikoko<br />

anali wodzikuza?<br />

3. Kodi pakati pa kukongola ndi khalidwe<br />

labwino, chofunika kwambiri n’chiyani?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

8


Nkhandwe ya Mtima Wangati Kuseri kwa<br />

Mphika<br />

Kalekalelo Nkhandwe inapita kukamwa madzi padziwe<br />

lina lomwe linali pafupi ndi phiri. Itafika kumeneko<br />

inaima chakumtunda n’kuyamba kupha ludzu.<br />

Itamwaza maso inaona Nkhosa, nayonso ikumwa<br />

madzi kumunsi kwa dziwelo. Kenako inayamba<br />

kuganiza kuti, “Ndikhozatu kutsuka m’kamwa ndi<br />

kandiwo kameneka. Nditangopeza chifukwa chabwino,<br />

ndikhoza kukaonetsa zakuda ndithu.” Ndiyeno itadya<br />

mutu inayamba kuyankhula mwaukali kwa Nkhosayo<br />

kuti, “N’chifukwa chiyani ukudetsa madzi amene<br />

ndikumwa?” Nkhosayo inayankha kuti, “Ayi, si ine.<br />

Ngati madziwo akubwera akuda kumeneko, vuto si ine<br />

ayi. Nokhanso mukuona kuti madziwa akuchoka<br />

kumeneko n’kumabwera kuno.” Kenako Nkhandwe ija<br />

inati, “Watero, chabwino, nanga n’chifukwa chiyani<br />

unkanditukwana chaka chatha chija nditabwera<br />

kudzamwa madzi kuno?” Nkhosayo inayankhanso<br />

kuti, “Si inenso ameneyo, inetu ndili ndi miyezi isanu<br />

ndi umodzi wokha, moti nthawi imeneyo ndinali<br />

ndisanabadwe.” Itamva zimenezi, Nkhandweyo<br />

inakwiya kwambiri ndipo inati, “Ndilibe nazo ntchito<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

9


zimenezo, ngati sunali iweyo ndiye kuti anali bambo<br />

ako.” Itangonena zimenezi inathamangira kunali<br />

Nkhosa kuja n’kuimbwandira, ndipo kenako inaidya.<br />

Phunziro: Munthu woipa sasowa chonamizira.<br />

Amachita chilichonse kuti akwaniritse cholinga chake<br />

ngakhale kupha munthu kumene.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi m’nthanoyi ndi nyama iti imene ili yoipa<br />

mtima? N’chifukwa chiyani mwayankha choncho?<br />

2. N’chifukwa chiyani mutu wa nkhaniyi<br />

ukuyerekeza mtima wa nkhandwe ndi kuseri kwa<br />

mphika?<br />

3. Perekani chitsanzo cha munthu woipa mtima<br />

yemwe anachitira mnzake zankhanza, ngakhale<br />

kuti mnzakeyo anali wosalakwa.<br />

4. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

10


Galu Apusitsidwa ndi Chithunzithunzi<br />

Tsiku lina Galu anatola nyama ndipo anaipana<br />

n’kumapita nayo kwawo kuti akaidye mwamtendere.<br />

Koma kuti akafike kwawo, ankafunika kuwoloka<br />

mtsinje wina, ndipo kuti awoloke mtsinjewo<br />

ankayenera kudutsa pamlatho waung’ono. Galuyo<br />

atayamba kuwoloka kudzera pamlathowo, anaona kuti<br />

m’madzi mukuoneka chithunzithunzi cha Galu<br />

atanyamula nyama kukamwa kwake. Ataona zimenezi,<br />

anaganiza kuti ameneyo ndi Galu wina. Chifukwa<br />

chosakhutira ndi nyama yomwe anali nayo, Galuyo<br />

anaganiza zolanda nyamayo kuti ikhalenso yake.<br />

Ndiyeno mwamphamvu, analumphira m’madzi muja,<br />

kuti khuvuu! Koma atangotsegula kukamwa kwake,<br />

nyama ananyamula ija inagwera m’madzi ndipo<br />

anaisakasaka koma sanaipeze. Pamenepo m’pamene<br />

anazindikira kuti Galu amaoneka mumtsinje uja<br />

chinali chithunzithunzi chake.<br />

Phunziro: Musalole kutaya zonse zomwe muli nazo kuti<br />

mupeze zinthu zomwe mukuganiza kuti mukhoza<br />

kuzipeza. Kumakhutira ndi zomwe muli nazo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

11


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Galuyu ankafunanso<br />

kulanda nyama ya Galu amene ankamuona<br />

m’madzi, kodi anali ndi njala?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti Galu angachitedi<br />

zimenezi? N’chifukwa chiyani mwayankha<br />

choncho?<br />

3. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

12


Mkango Unatenga Zonse<br />

Tsiku lina Mkango unapita kosaka limodzi ndi Agalu<br />

am’tchire atatu. Nyama zimenezi zinasaka, kusaka,<br />

kenako n’kusaka koma sizinagwire kanthu. Ndiyeno<br />

mwamwayi, nyamazi zinasokolotsa Mphalapala ndipo<br />

posakhalitsa zinaigwira n’kuipha. Zitatere, Agalu<br />

am’tchirewo anayamba kunena kuti, “M’pofunika kuti<br />

tonse tigawane nyamayi mofanana.” Koma Mkango<br />

unabangula n’kuuza Agaluwo kuti, “Dulani nyamayi<br />

panayi!” Agalu aja anamveradi zimenezo ndipo<br />

anasenda nyamayo n’kuidula panayi. Kenako Mkango<br />

uja unaima patsogolo pa nyamayo n’kuyamba<br />

kulongosola za kagawidwe kake. Unati: “Mbali<br />

yoyambayi ikhala yanga chifukwa ndine Mfumu ya<br />

Zinyama zonse m’nkhalango muno. Mbali yachiwiriyi<br />

ikhalanso yanga chifukwa ndine ndinayambitsa<br />

ulenjewu. Pomwe mbali yachitatuyi ikhalanso yanga<br />

chifukwa ndinathamangitsa nawo nyamayi. Koma<br />

ponena za mbali yotsalayo, amene ali wolimba mtima<br />

ayerekeze kuigwira aone . . . . ” Atamva zimenezi,<br />

Agalu am’tchirewo anadzuma chapansipansi ndipo<br />

kenako ananyamuka n’kumapita, kwinaku atapanira<br />

michira yawo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

13


Phunziro: Mukhoza kuthandiza anthu amphamvu<br />

kuchita zinazake, koma simungadye nawo zimene<br />

angapeze.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Agalu am’tchire ankathawa<br />

atapanira michira?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti Agaluwo ankayenera<br />

kudya nawo nyamayo? N’chifukwa chiyani<br />

mukutero?<br />

3. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

14


Dokowe Apulumutsa Nkhandwe<br />

Tsiku lina Nkhandwe inali ndi njala zedi ndipo<br />

inagwira nyama n’kuyamba kuipwepweta<br />

mwankhanza. Koma mwatsoka fupa linaima pammero,<br />

moti inkalephera kulimeza. Nkhandweyo inayamba<br />

kumva ululu woopsa ndipo inkabuula kwinaku<br />

ikupempha nyama zina kuti aithandize. Koma<br />

chifukwa cha khalidwe lake la umadyera mphoto,<br />

nyama zina zinkachita mantha, moti palibe inalimba<br />

mtima kuithandiza. Kenako Nkhandweyo inayamba<br />

kunyengerera aliyense amene inkakumana naye<br />

n’cholinga choti aipulumutse. Inkati, “Ndikupatsani<br />

chilichonse chimene mukufuna ngati mutandichotsa<br />

fupali kukhosiku.” Mwamwayi, Dokowe anavomera<br />

kuti ayesa kuchotsa fupalo, ndipo anaiuza kuti igone<br />

pansi n’kutsegula kukamwa kwake. Dokoweyo<br />

anapisa kukhosi kwa Nkhandweyo ndi mulomo wake<br />

ndipo khosi lake lonse lalitalilo linalowa m’kamwa<br />

mwa Nkhandweyo. Dokoweyo anakwanitsadi kuchotsa<br />

fupalo ndipo Nkhandweyo inayamba kupeza bwino.<br />

Ndiyeno Dokowe anauza Nkhandweyo kuti, “Tsopano<br />

popeza ndachotsa fupali, ndininkhenitu zimene<br />

munalonjeza zija. Pajatu lonjezo linadulitsa mutu wa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

15


nkhuku!” Itamva zimenezi, Nkhandweyo inamwetulira<br />

n’kuonetsa mano ake, ndipo kenako inati,<br />

“Muziyamika a Dokowe. Inuyotu munalowetsa mutu<br />

wanu m’kamwa mwanga n’kuutulutsamo uli<br />

bwinobwino, popanda vuto lililonse. Ndiye mukuti<br />

mukufuna ndikupatseninso mphoto ina kuposa<br />

imeneyo?”<br />

Phunziro: Munthu wadyera sayamika.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />

Dokowe anathandiza Nkhandwe?<br />

2. N’chifukwa chiyani Dokowe anauza Nkhandwe<br />

kuti imupatse zimene inalonjeza?<br />

3. Kodi mukuganiza kuti Nkhandwe inaperekadi<br />

mphoto kwa Dokowe? N’chifukwa chiyani<br />

mukutero?<br />

4. Tiyerekeze kuti Nkhandweyo inakana kupereka<br />

mphoto kwa Dokowe, kodi tinganene kuti<br />

inalakwa?<br />

5. N’chifukwa chiyani tiyenera kumachitadi<br />

zimene talonjeza?<br />

6. Kodi nkhaniyi ikutiphunzitsa chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

16


<strong>Mpandamachokero</strong><br />

Kalelo, pamudzi wina panali mkamwini wina yemwe<br />

ankasakasaka chifukwa chopitira kwawo. Anthu a<br />

pamudzipo ankakhala naye bwino zedi. Koma kenako<br />

munthuyu anatopa ndi ulemu, ndipo anayamba<br />

kusakasaka chifukwa chochokera pakhomopo. Ndiye<br />

tsiku lina, ana ankaphika masanje ndipo mkamwiniyo<br />

anapita pomwe anawo anakoleza moto wawo<br />

n’kuukodzera. Anawo anayamba kulira ngati kuti wina<br />

wawatsina, moti akuluakulu a pamudzipo anatuluka<br />

m’nyumba kuti akaone chomwe chachitika. Atafunsa<br />

anawo kuti chachitika n’chiyani, anaulula kuti<br />

mkamwiniyo wawazimitsira moto wawo komanso kuti<br />

anachita kuukodzera. Akuluakuluwo anakhumudwa<br />

kwambiri ndipo anapita kunyumba kwa mkuluyo kuti<br />

akamufunse za nkhaniyo. Atafika, mkamwiniyo<br />

anawalandira n’kuwalowetsa m’nyumba. Anthuwo<br />

anapepesa chifukwa chobwera mwadzidzidzi, koma<br />

mkamwiniyo anati, “Ayi, mwafika mwatha.” Ndiye<br />

kenako anawauza kuti, “Tikupunguleni mpweya!”<br />

Zitatero anthu a pamudzipo anayamba kuyala nkhani<br />

yonse. Koma mkamwiniyo atamva zimene anthuwo<br />

ananena, anakwiya kwambiri ndipo anati: “Zoona<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

17


mmene ndakuliramu ndingakodzere moto wa ana?<br />

Anthu inutu simukundifuna pamudzi pano. Basi<br />

ndikupita kwathu.” Kenako anamanga nsanza zake<br />

pachitenje, n’kunyamuka kumapita kwawo.<br />

Phunziro: Anthu ena akatopa kukhala pamalo,<br />

amachita kusakasaka chifukwa chochokera.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi vuto la mkamwiniyu linali chiyani?<br />

2. Kodi pali umboni wanji wosonyeza kuti anthu a<br />

pamudziwu anali abwino?<br />

3. Kodi mukuganiza kuti mkamwiniyo<br />

ankatanthauza chiyani pamene ananena kuti,<br />

“tikupunguleni mpweya”?<br />

4. Kodi mwambi wakuti, “mpandamachokero<br />

adakodzera moto wa ana” unayamba bwanji?<br />

5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

18


Kusamvana Pakati pa Munthu ndi Njoka<br />

Mwana wa Mlimi wina anaponda mchira wa Njoka<br />

mwangozi, ndipo Njokayo inalusa n’kumugagada, moti<br />

anafera pomwepo. Bambo a mwanayo atamva zimenezi<br />

anakwiya zedi, ndipo ananyamula nkhwangwa<br />

n’kuyamba kuthamangitsa Njokayo. Ataipeza<br />

anaponya nkhwangwayo ndipo anaidula mchira.<br />

Zimenezi zinachititsa kuti njokayo ikwiye zedi, moti<br />

inaganiza zokhaulitsa mlimiyo. Inanyamuka n’kupita<br />

m’khola la mlimiyo n’kukaluma ng’ombe zonse, moti<br />

inasiya mlimiyo manja ali m’khosi, ng’ombe zake zonse<br />

zitafa. Koma kenako mlimiyo anaona kuti kubwezera<br />

sikuthandiza, ndipo anaganiza zokambirana ndi<br />

Njokayo kuti akhazikitse mtendere. Choncho tsiku lina<br />

Mlimiyo anauyamba ulendo wopita kwa Njokayo<br />

atatenga kaphoso ka chakudya komanso uchi, ndipo<br />

atafika anaika zinthuzo pauna wa Njoka n’kuodira.<br />

Njoka itatuluka, Mlimiyo anati, “M’bale wanga njoka,<br />

tiye tiiwale zakale. Ndikuona kuti n’zomveka kuti<br />

unalanga mwana wanga atakuchitira chipongwe.<br />

Komanso n’zomveka kuti unapha ng’ombe zanga<br />

utakwiya chifukwa chodulidwa mchira. Komabe,<br />

popeza ndine bambo wa mwana unapha uja,<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

19


sindinalakwe kukudula mchira chifukwa monga<br />

ukudziwira, imfa ya mwana imakhala yowawa<br />

kwambiri. Ndiye popeza aliyense wakhutira ndi zimene<br />

wachitira mnzake, tiye tiiwale zakale n’kuyambiranso<br />

kugwirizana.” Pamenepo Njokayo inati: “Ayi,<br />

sindikufuna. Pita nazo uko zinthu zakozo! Ndikudziwa<br />

kuti sungaiwale imfa ya mwana wako, komanso ineyo<br />

sindingaiwale za mchira wanga, womwe iweyo<br />

unaudula mopanda chisoni.”<br />

Phunziro: Nthawi zina zimatheka kukhululukira<br />

munthu, koma osaiwala zomwe anakuchitira.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Mlimi anatenga chakudya<br />

komanso uchi popita kukakumana ndi Njoka?<br />

2. N’chifukwa chiyani Njoka inakana kulandira<br />

mphatso zomwe Mlimiyo anapititsa?<br />

3. Kodi zimene Njokayo inachita ndi zabwino?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

20


Khoswe Wam’tauni ndi Khoswe<br />

Wakumudzi<br />

Kalekalelo Khoswe Wam’tauni anapita kukacheza kwa<br />

msuweni wake, yemwe ankakhala kumudzi. Khoswe<br />

Wakumudziyo anasangalala kwambiri ndi zimenezi<br />

moti anamulandira ndi manja awiri mnzakeyo.<br />

Ngakhale kuti analibe zinthu zambiri, Khoswe<br />

Wakumudziyo anayesetsa kukonzera mnzakeyo<br />

chakudya chabwino. Mwachidule tingoti anamupatsa<br />

zonse zomwe akanakwanitsa. Anamupatsa nyemba,<br />

nyama, mabanzi komanso mtedza. Ndiyeno Khoswe<br />

Wam’tauni uja anasolola mphuno yake n’kuyamba<br />

kununkhiza mosonyeza kuti chakudyacho<br />

chikumunyansa, ndipo kenako anati: “Asuweni<br />

sindimakumvetsani. Kodi mumakwanitsa bwanji<br />

kudya chakudya ngati chimenechi? Koma m’pomveka,<br />

kunoko n’kotsalira kwambiri moti simungakwanitse<br />

kupeza zakudya zonona komanso zabwinozabwino<br />

zomwe zimapezeka m’tauni. Tiyeni tipite kwathu<br />

ndikakuonetseni kukoma kwa moyo. Mukakangokhala<br />

sabata imodzi, mukaona kuti moyo womwe<br />

mukukhala kunowu ndi wofanana ndi kukhala<br />

kundende.” Nthawi yomweyo makoswe awiriwo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

21


anauyamba ulendo wopita m’tauni ndipo anafika<br />

usiku kwambiri kunyumba kwa Khoswe Wam’tauni<br />

uja. Kenako Khoswe Wam’tauniyo anati: “Ukuoneka<br />

kuti waweyeseka ndi ulendo, bwanji ndikupatseko<br />

zokhwasulakhwasula? Tabwera kuno!” Kenako<br />

anagwira mnzakeyo dzanja n’kuyamba kumukoka<br />

kupita naye kuchipinda chodyera. Kumeneko anapeza<br />

kuli zinthu zambiri zomwe zinatsala patebulo moti<br />

sanachedwenso ayi, koma kuyamba kudya makeke<br />

komanso zakudya zina zokhetsa dovu, zomwe<br />

anazipeza m’chipindacho. Koma mwadzidzidzi,<br />

anamva agalu akuuwa. Ndiyeno Khoswe Wakumudzi<br />

anafunsa kuti, “Kodi chimenecho n’chiyani?”<br />

Mnzakeyo anayankha kuti, “Aa, usaope. Amenewo ndi<br />

agalu a m’nyumba muno.” Ndiyeno Khoswe<br />

Wakumudziyo anati, “Wati ndisaope? Kwathu<br />

ndimadya mwamtenderetu ine, moti phokoso limenelo<br />

silikundisangalatsa.” Posakhalitsa chitseko<br />

chinatseguka mwamphamvu ndipo Agalu akuluakulu<br />

awiri anatulukira. Makoswe awiriwo atangoona<br />

agaluwo, anayamba kuthawa pofuna kupulumutsa<br />

miyoyo wawo. Kenako Khoswe Wakumudzi anati,<br />

“Msuweni, ine ndikupita kwathu.” Khoswe<br />

Wam’tauniyo anafunsa mnzakeyo kuti, “Bwanji,<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

22


ukufuna kubwerera kumudzi nthawi yomweyi?” Koma<br />

Khoswe Wakumudziyo anati, “Inde, ndikupita. Bola<br />

ndizikadya nyemba komanso mabanzi ndili<br />

pamtendere, kusiyana n’kumadya makeke komanso<br />

zinthu zonona ndili ndi mantha.”<br />

Phunziro: “Ndi bwino kumadya chisoso pali mtendere,<br />

kusiyana ndi kumadya nyama uli ndi mantha.”<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Khoswe Wakumudzi<br />

anapita m’tauni?<br />

2. N’chifukwa chiyani khosweyu anabwerera<br />

kumudzi?<br />

3. Kodi pali kusiyana kotani pakati pa Khoswe<br />

Wakumudzi ndi Khoswe Wam’tauni?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

23


Nkhadwe Inapusitsa Khwangwala<br />

Tsiku lina Nkhandwe inaona Khwangwala akuuluka.<br />

Khwangwalayo anali atapana nyama kukamwa kwake.<br />

Posakhalitsa Khwangwalayo anatera mumtengo wina<br />

ndipo Nkhandwe inaganiza kuti, “Ndikhozatu<br />

kumuyeretsa m’maso ameneyu.” Kenako inanyamuka<br />

n’kupita pafupi ndi mtengo anatera Khwangwala uja<br />

n’kunena kuti, “Muli bwanji Mayi Khwangwala?<br />

Mukuonekatu bwino lero. Mwatchena suti yokongola<br />

zedi, yomwenso ikugwirizana ndi kakolala koyera<br />

komwe kali m’khosi mwanuko. Mukuonekanso kuti<br />

mukhoza kuimba mwanthetemya kuposa mbalame<br />

zina zonse. Ndiponsotu mawu anu amandisangalatsa<br />

zedi, moti mungachite bwino mutandiimbira kanyimbo<br />

mumakonda kuimba kaja, . . . kamene kaja.<br />

Mukangochita zimenezi, nthawi zonse ndizikupatsani<br />

moni waulemu monga Mfumukazi ya Mbalame zonse.”<br />

Khwangwalayo atamva zimenezi anapusitsika ndipo<br />

anatukula mutu wake n’kuyamba kuimba, amvekere<br />

khwaa! khwaa! khwaa! Koma atangochita zimenezi,<br />

nyama inali kukamwa kwake ija inagwera pansi ndipo<br />

Nkhandwe ija inatola n’kunena kuti, “Zikomo<br />

kwambiri mayi. Zimene ndimafuna ndi zimenezi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

24


Monga malipiro a nyama ndatengayi, ndikupatsani<br />

malangizo oti adzakuthandizeni m’tsogolo.<br />

Mukadzaona munthu akukutamandani pa chifukwa<br />

chosadziwika bwino, mudzadziwe kuti akufuna<br />

kukupondani.”<br />

Phunziro: Osamakhulupirira anthu achinyengo.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi ndi ndani amene anali tambwali pakati pa<br />

Nkhandwe ndi Khwangwala?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inapempha<br />

Khwangwala kuti amuimbire nyimbo?<br />

3. Nanga n’chiyani chimene chinakopa<br />

Khwangwala kuti aimbedi nyimboyo?<br />

4. Kodi n’zoona kuti Khwangwala analidi<br />

mbalame yokongola komanso yodziwa kuimba?<br />

5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

25


Mkango Udwala Mwakayakaya<br />

Nthawi ina Mkango unakalamba kwambiri moti<br />

unayamba kudwala mwakayakaya pakhomo la phanga<br />

lake. Mkangowo unkangokhalira kubuula tsiku lonse<br />

ndiponso unkavutika kupuma. Nyama zina za<br />

m’nkhalango zinabwera kudzazonda matendawo koma<br />

popeza Mkango ndi nyama yoopsa, zinaima chapatali<br />

ndithu. Koma zitaona kuti Mkangowo ulibenso<br />

mphamvu komanso kuti moyo wake wangotsala madzi<br />

amodzi, zinayamba kuyandikira pang’onopang’ono.<br />

Zina mwa nyamazo zinayamba kuganiza kuti,<br />

“Tsopano nthawi yakwana yoti tibwezere zonse zimene<br />

Mkango unatichitira.” Ndiyeno Nguluwe inathamanga<br />

n’kukagunda Mkangowo. Kenako Njati nayonso<br />

inadzambatuka n’kukaubaya ndi nyanga zake. Koma<br />

palibe chimene Mkangowo unachita, unangogona<br />

pansi kwala! Choncho, Bulu ataona kuti Mkango<br />

sungachite kanthu, anapita pafupi ndi Mkangowo<br />

n’kuyamba kuvina kwinaku akugwedezera mchira<br />

wake, ndipo kenako anamenya Mkangowo ndi<br />

miyendo yake yakumbuyo. Mkangowo utaona zimenezi<br />

unalira modandaula kuti, “Apa ndiye ndifa kawiri<br />

ndithu. Zoona kumenyedwa ndi ana omwe?”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

26


Phunziro: Ndi anthu amatha amene amalimbana ndi<br />

munthu wamphamvu akamatsirizika.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani nyamazi zinkayandikira<br />

pang’onopang’ono?<br />

2. N’chifukwa chiyani nyama zina zinaukira<br />

Mkango?<br />

3. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Bulu<br />

anapita komalizira?<br />

4. Kodi kubwezera n’kulakwa?<br />

5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

27


Bulu Komanso Galu<br />

Tsiku lina Mlimi anapita kukaona ana komanso ziweto<br />

zake. Pakati pa nyamazi panali Bulu. Ndiye pamene<br />

Mlimiyo ankapita kumeneku, n’kuti ali limodzi ndi<br />

Galu wake yemwe ankamukonda kwambiri. Galuyo<br />

ankadumphadumpha n’kumanyambita komanso<br />

kugwira mkono wa Mlimiyo. Kenako Mlimiyo anapisa<br />

m’thumba n’kutenga chakudya n’kupatsa Galuyo,<br />

ndipo kenako anakhala pansi n’kuyamba kupereka<br />

malangizo kwa ana ake. Ndiyeno Galuyo analumphira<br />

pamiyendo pa Mlimiyo ndipo Mlimiyo anayamba<br />

kumusisita. Bulu uja ataona zimenezi anasilira<br />

kwambiri moti anadula chingwe chimene<br />

anamumanga nacho n’kuthamangira kwa Mlimiyo kuti<br />

nayenso akachite chimodzimodzi. Mlimiyo ataona<br />

zimenezi anayamba kuseka ndipo Buluyo ankaganiza<br />

kuti zimene akuchitazo zikumusangalatsa. Ndiye<br />

kenako anaganiza zoti alumphire pamiyendo pa<br />

Mlimiyo n’cholinga choti nayenso amusisite. Koma<br />

chifukwa cha kutalika, Buluyo sanakwanepo, moti<br />

miyendo yake inagwira m’mapewa mwa Mlimiyo. Ana a<br />

Mlimiyo ataona zimenezi anaganiza kuti Buluyo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

28


wachita misala, ndipo anatenga ndodo n’kuyamba<br />

kumuumbudza.<br />

Phunziro: Osamangotengera zilizonse zimene ena<br />

akuchita.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Bulu anaganiza zotengera<br />

zochita za Galu?<br />

2. Kodi Buluyo anakumana ndi zotani? Nanga<br />

n’chifukwa chiyani anakumana ndi zimenezo?<br />

3. Kodi n’kulakwa kumangotengera zochita za<br />

ena, bola ngati tikuona kuti zikuwayendera bwino?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

29


Khoswe Apulumutsa Mkango<br />

Tsiku lina Mkango ukugona, Khoswe anayamba<br />

kuukwerakwera. Zimenezi zinachititsa kuti Mkangowo<br />

udzidzimuke ndipo unagwira Khosweyo n’kutsegula<br />

kamwa lake kuti ungomuponyera m’kamwa<br />

n’kumutafuna. Koma Khosweyo anakuwa n’kuuza<br />

Mkangowo kuti, “Pepani Mfumu yanga,<br />

ndikhululukireni chonde! Ndimvereni chisoni, ndinetu<br />

mwana wamasiye! Mutandisiya wamoyo kano kokha,<br />

ndikhoza kudzakupulumutsani m’tsogolo!” Mkango<br />

utamva zimenezi unafa nalo phwete ndipo unati,<br />

“Usandiseketse m’kamwa, zoona iweyo kuchepa<br />

kumeneku ungandipulumutse?” Posakhulupirira<br />

zimenezi, Mkangowo unamusiyadi Khosweyo. Ndiyeno<br />

patapita nthawi, Mkango uja unagwidwa pamsampha,<br />

ndipo alenje atauona anaganiza zounyamula n’kupita<br />

nawo kwa mfumu yawo. Kenako anaugwira<br />

n’kuukwidzinga pamtengo n’kupita kukasakasaka<br />

ngolo yoti adzaunyamulire. Alenje aja atangochoka,<br />

Khoswe uja anadutsa pafupi ndi pomwe panali<br />

Mkango uja. Ataona mmene Mkangowo<br />

unkandandaulira, anapita pomwepo n’kuchecheta<br />

chingwe chomwe anaumangira chija, ndipo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

30


chinaduka. Kenako anauza Mkangowo kuti, “Si paja<br />

ndinakuuzani kuti ndikhoza kudzakupulumutsani!<br />

Mwaonatu, osamachepetsa kolemera.” Kenako<br />

ananyamuka n’kumapita.<br />

Phunziro: Nthawi zina anthu onyozeka ndi amene<br />

amathandiza kwambiri.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Mkango unasiya Khoswe<br />

kuti apite?<br />

2. Kodi Khoswe anathandiza bwanji Mkango?<br />

Nanga n’chifukwa chiyani anauthandiza?<br />

3. Pakati pa Khoswe ndi Mkango, kodi<br />

mukuganiza kuti ndi nyama iti imene<br />

inaphunzirapo kenakake?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

31


Namzeze Achenjeza Mbalame Zina<br />

Nthawi ina Mlimi anapita kukafesa mbewu ya chamba<br />

m’munda wina womwe Mbalame zinkakonda kukatola<br />

zakudya zake. Ndiye Mbalame ina yotchedwa Namzeze<br />

itaona zimenezi, inayamba kuchenjeza mbalame<br />

zinzake zomwe zinkatola zakudya m’mundawo. Inati,<br />

“Samalani ndi munthu uyo!” Mbalame zinazo<br />

zinamufunsa kuti, “Chifukwa? Kodi zimene akuchitazo<br />

ife zikutikhudza?” Iye anayankha kuti, “Munthuyu<br />

akufesa mbewu yoipa. Musayerekeze kusiya nthangala<br />

ngakhale imodzi ya mbewu zimenezi. Mukapanda<br />

kutero, mudzaona zakuda!” Mbalamezo zinkaona kuti<br />

zimene Namzeze ankakambazo ndi za kuntchini<br />

kwadzaza, moti sizinatsatire malangizowo. Koma<br />

patapita nthawi, mbewuzo zinayamba kukula ndipo<br />

mbalamezo zinayamba kuthothola masamba ake<br />

n’kumakamangira zisa. Pamene mbewu zija zinkacha,<br />

mbalame zosamverazo zinagwidwa zili m’zisa<br />

zopangidwa ndi masamba a chamba, omwe zinatenga<br />

m’munda uja. Mbalame zambiri zinasokonezeka ndi<br />

tsokali ndipo sizinkadziwa chifukwa chimene<br />

munthuyo ankatengera zisa zawo. Ndiyeno Namzeze<br />

anaziuza kuti, “Ndinakuuzani chiyani ine?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

32


Kumachotseratu mbewu yoipa isanamere! Mtsinje wa<br />

tinkanenatu unathera mu si izi.”<br />

Phunziro: Kumachotsa mbewu yoipa isanamere, apo<br />

ayi m’tsogolo imadzabweretsa mavuto.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mbewu yoipa imene namzeze ankanena<br />

inali chiyani? N’chifukwa chiyani mukutero?<br />

2. Kodi namzeze anauza mbalame zinzake kuti<br />

zichite chiyani?<br />

3. N’chifukwa chiyani Mlimiyo ankatenga zisa za<br />

mbalamezo?<br />

4. Kodi mungapereke zitsanzo za zinthu zina<br />

zoipa zimene ngati titazilekerera zikhoza<br />

kutibweretsera mavuto?<br />

5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

33


Achule Afuna Mfumu<br />

Achule ankakhala mosangalala m’dambo lina<br />

lokongola kwambiri. Nthawi zonse ankangokhalira<br />

kusewera. Ankati akadzuka m’mawa, ankayamba<br />

kuwothera dzuwa komanso kudya, ndipo akamva<br />

kutentha, ankakwera pamwala n’kudziponya m’madzi<br />

kuti mphavaa! Ankakhala kukhosi kuli mbee ndipo<br />

palibe chimene chinkawavutitsa. Komatu ukakhala<br />

pabwino, poipa pamakuitana. N’kupita kwa nthawi<br />

Achulewa anayamba kuona kuti moyo umenewu si<br />

wabwino, moti ankafuna atakhala ndi mfumu<br />

komanso malamulo abwino oti aziyendera. Choncho<br />

anaganiza zokapempha kwa Mulungu kuti awapatse<br />

mfumu yoti iziwalamulira. Iwo anati, “Mulungu wathu<br />

wamkulu, titumizireni mfumu yoti izitilamulira<br />

komanso kutipatsa malamulo oti tiziyendera.”<br />

Mulungu atamva zimene Achulewo ananena, anaseka<br />

ndipo anagwetsa chipika chachikulu chomwe<br />

chinagwera m’dziwe lomwe linali m’dambo lija.<br />

Achulewo anachita mantha kwambiri chifukwa cha<br />

phokoso lomwe linamveka pamene chipikacho<br />

chinkagwera m’madzi, moti onse anathawa n’kupita<br />

kumtunda. Kwa masiku ambiri, Achulewo ankakhala<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

34


mwamantha ndipo sankayandikira n’komwe chinthu<br />

choopsa chomwe chinagwera m’madzicho. Koma<br />

patapita nthawi, achulewo anaona kuti chinthucho<br />

sichikutakataka. Ndiyeno Achule ena olimba mtima<br />

anapita pafupi ndi chipika chija, moti ena analimba<br />

mtima n’kuchigwira. Komabe, chipikacho<br />

sichinasunthe. Kenako Chule wina, yemwe<br />

ankadziwika kuti ndi wolimba mtima kwambiri,<br />

analumphira pamwamba pachipikacho n’kuyamba<br />

kuvina, ndipo Achule enanso anayamba kuchita<br />

zomwezo. Izi zitachitika, Achulewo anatha mantha<br />

ndipo anayambanso kukhala monga mmene<br />

ankakhalira kale. Anaiwaliratu zoti Mulungu<br />

anawagwetsera chipika, chomwe chinali ngati mfumu<br />

yawo. Achulewo anayamba kuona kuti mfumuyi ndi<br />

yatulo ndiponso kuti ndi yosawayenera, moti<br />

anaganiza zopitanso kwa Mulungu kuti<br />

akapemphenso mfumu ina. Anati, “Tikufuna mfumu<br />

yeniyeni yoti izitilamulira, osati yomwe ikungoliza<br />

mkononoyi!” Zimenezi zinachititsa kuti Mulungu<br />

akwiye ndipo anatumiza Dokowe. Dokoweyo<br />

anayamba kujompha achulewo n’kumawadya.<br />

Achulewo ataona zimenezi, anachita mantha zedi moti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

35


anayamba kulirira Mulungu kuti awachotsere<br />

chilombocho, koma munali m’mbuyo mwa alendo.<br />

Phunziro: Ndibwino kukhala popanda mfumu<br />

n’kumakhala bwinobwino kusiyana ndi kukhala nayo,<br />

koma n’kukhala yankhanza.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />

Mulungu anatumiza chipika kwa Achule aja,<br />

m’malo mowapatsa mfumu yeniyeni?<br />

2. N’chifukwa chiyani achule anapitanso<br />

kukapempha mfumu ina?<br />

3. Kodi zangati zimene zinachitikira achulewa<br />

zimachitikanso masiku ano?<br />

4. N’chifukwa chiyani Mulungu anawakwiyira?<br />

5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

36


Phokoso la Mapiri<br />

Tsiku lina anthu a m’mudzi wina anayamba kumva<br />

phokoso loopsa lomwe linkamveka kuchokera<br />

m’Mapiri ena omwe anali pafupi ndi kwawo. Anthuwa<br />

ankaganiza kuti Mapiriwo akubereka ana. M’Mapiriwo<br />

munkatuluka chiutsi, nthaka inkangoti teketeke,<br />

mitengo inkangogwa komanso miyala inkangosweka.<br />

Iwo ankaona kuti pakhoza kuchitika chinachake<br />

choopsa. Anthuwo anasonkhana pamodzi kuti aone<br />

chomwe chitachitike. Anadikira, kudikira n’kudikira,<br />

koma palibe chinachitika. Kenako panachitikanso<br />

chivomerezi china champhamvu kwambiri moti<br />

nthaka inang’ambika pambali pa phiri lina. Anthuwo<br />

anayamba kuyang’ana mwachidwi m’phangalo ndipo<br />

anapitirizabe kudikira. Kenako anangoona kakhoswe<br />

kakang’ono kakuchokera m’phangalo. Kakhosweko<br />

kankapukuta mutu wake ndi timiyendo take<br />

tating’ono. Kenako kanatuluka n’kumalowera kumene<br />

kunali anthu aja. Kungochokera nthawi imeneyo<br />

anthuwo anayamba kunena kuti, “Pakakhala<br />

chiphokoso chachikulu, zotsatira zake zimakhala<br />

zogwetsa mphwayi.” Ndipo ena ankati, “N’chifukwa<br />

chaketu anthu a kum’mawa amanena kuti, ‘Chidebe<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

37


chopanda kanthu chimapanga phokoso kwambiri.’<br />

Mpake kuti ena amaganiza kuti, ‘anthu omwe<br />

sayankhulayankhula ndi amene amaganiza<br />

mwaphokoso zedi!”<br />

Phunziro: Nthawi zina anthu amene amalongolola<br />

kwambiri sachita zanzeru.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Anthu ankaganiza kuti chichitike<br />

n’chiyani?<br />

2. Kodi zimene Anthuwo ankayembekezera<br />

zinachitikadi?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

38


Akalulu Akumana Ndi Mavuto<br />

Nthawi inayake Akalulu ankazunzidwa ndi zilombo<br />

zina zosadziwika bwinobwino moti ankasowa<br />

kothawira. Zimenezi zinachititsa kuti akangoona<br />

nyama iliyonse azithawa n’kukabisala. Akaluluwa<br />

anafika potopa ndi zimenezi moti tsiku lina anaganiza<br />

zokangodziponya m’madzi n’kufa. Ndiye ataona Njati<br />

zikuthamanga, Akaluluwo anathawira kudziwe lina<br />

kuti akangodziponya m’madzi n’kulekana nawo moyo<br />

wokhala mwamantha. Ndiye atayandikira dziwelo,<br />

anadzidzimutsa Achule ena omwe ankaothera dzuwa<br />

ndipo nthawi yomweyo Achulewo anadziponya<br />

m’madzi. Kalulu wina ataona zimenezo anati, “Aa!<br />

akuluakulu, mavuto amene tili nawo ifewa, bola.<br />

Taonani anzathuwa! Ndaphunzirapo kanthu.<br />

Ukamakumana ndi mavuto, kumakumbukira kuti pali<br />

ena omwe akukumana ndi mavuto onenepa kwambiri<br />

kuposa ako.”<br />

Phunziro: Ukamakumana ndi mavuto, m’malo<br />

mongoganiza zodzipha, ndi bwino kumakumbukira kuti<br />

pali enanso amene akukumana ndi mavuto kuposa<br />

akowo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

39


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Akalulu ankafuna<br />

kudziponyera m’madzi?<br />

2. N’chiyani chinawapangitsa kusintha maganizo?<br />

3. Kodi ndi nyama ziti zimene mukuona kuti<br />

nazonso zimachita mantha kwambiri zikaona<br />

Achule?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

40


Ukakwera M’mwamba Usamatukwane<br />

Pansi<br />

Mnyamata wina anakwera padenga la nyumba ndipo<br />

atayang’ana pansi, anaona Nkhandwe ikudutsa pafupi<br />

ndi nyumbayo. Nthawi yomweyo anayamba<br />

kuinyogodola amvekere, “Ndiwe chigawenga komanso<br />

kapsala. N’chifukwa chiyani wabwera kuno kunyumba<br />

za anthu amtendere komanso abwino, kodi ulibe<br />

manyazi? N’chifukwa chiyani umakonda kupita<br />

m’malo amene anthu amadziwa kale makhalidwe ako<br />

ochititsa dambisi?” Itamva zimenezi, Nkhandweyo<br />

inayankha kuti, “Ukhoza kundinyoza mmene<br />

ungathere. Zimakhala zophweka kumadzitukumula<br />

komanso kumachita mwano utakwera padenga.<br />

Ndikulakalaka kuti tsiku lina uzidzabwebwetuka<br />

choncho uli pansipa.”<br />

Phunziro: Osamatha mawu zikakhala kuti zinthu<br />

zikukuyendera. Osamachita chipongwe ukakhala malo<br />

otetezeka, chifukwa nthawi ina udzachokapo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

41


Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />

Mnyamatayu ankanyoza Nkhandwe ali padenga la<br />

nyumba?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti nthawi zina anthu<br />

amachitadi zangati zimenezi? Perekani chitsanzo.<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

42


Pansi pa Mtima<br />

Tsiku lina Gondwa anaba nkhuku pakhomo lina ndipo<br />

anakalowa nayo kuphanga lake. Atafika kuphangako<br />

anauza ana ake kuti waba nkhukuyo kukhomo<br />

lapafupi. Koma kuti aiwotche, ankafunika moto. Ndiye<br />

Gondwayo anaganiza zotuma mwana wake kuti<br />

akapale moto kukhomo anaba nkhuku lija. Anamuuza<br />

kuti, “Ndikufuna ukapale moto uko. Koma popeza<br />

nkhukuyi taba komweko, asakadziwe kuti tikufuna<br />

kudzawotchera nkhuku. Ndiye ngakhale<br />

akakukakamize, usakaulule kuti motowo<br />

tikudzachitira chiyani. Koma pansi pamtima<br />

uzingodziwa iweyo kuti tikufuna kudzawotchera<br />

nkhuku.” Kenako mwanayo ananyamuka n’kupita<br />

kukapala moto atatenga chiwaya chake. Atafika<br />

kumeneko, anagogoda ndipo ananena chimene<br />

wabwerera. Anthu amene anawapeza kunyumbako<br />

anayamba kumupanikiza ndi mafunso, amvekere,<br />

“Motowo mukufuna mukachite nawo chiyani?”<br />

Mwanayo anayankha kuti, “Anandiuzatu kuti<br />

ndisadzaulule. Amati ndizingodziwa ndekha, pansi<br />

pamtima wanga, kuti tikufuna kukawotchera<br />

nkhuku.” Anthuwo atangomva zimenezi anazindikira<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

43


kuti nkhuku yawo waba ndi Gondwa, ndipo<br />

anathamangitsa mwanayo mpaka kukafika paphanga<br />

lija. Kenako anatenga khasu n’kukumba phangalo<br />

ndipo anapha Gondwa ndi ana ake onse.<br />

Phunziro: Palibe chinsinsi padziko lapansi.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mwana wa Gondwa ananena chiyani<br />

atafunsidwa chifukwa chimene anapitira kukapala<br />

moto?<br />

2. Kodi zimene mwanayo ananena zinali zoona<br />

kapena zabodza?<br />

3. Kodi mwanayu analakwitsa kunena zinthu zina<br />

zimene bambo ake anamuuza kuti angozidziwa<br />

yekha? Ndiye tinganene kuti kunena zoona si<br />

kwabwino?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

44


Njoka Yopanda Pabwino<br />

Chaka china kunazizira kwambiri moti madzi ankatha<br />

kuuma gwa ngati mwala. Ndiye munthu wina, yemwe<br />

ankachokera kunkhalango, anaona njoka yakuda<br />

itagona m’mbali mwa nsewu. Njokayo inkaoneka kuti<br />

yangotsala pang’ono kutsirizika chifukwa cha kuzizira.<br />

Kenako munthuyo anaichitira chifundo ndipo anaitola<br />

n’kuiika mujuzi yake kuti imve kutentha. Atafika<br />

kwawo anaiika pafupi ndi moto kuti itenthedwe. Ana a<br />

munthuyo ankangoiyang’ana. Kenako Njokayo<br />

inayamba kumvako bwino, moti inayambiranso<br />

kuyenda bwinobwino. Ndiyeno mwana m’modzi<br />

anaganiza zoti aisisite, koma atangochita zimenezi,<br />

Njokayo inadzutsa mutu wake kuti imulume.<br />

Munthuyo atangoona zimenezo anatenga nkhwangwa<br />

yake n’kudula Njokayo pakati. Kenako anati, “Anthu<br />

ena alibe pabwino inu! Ukhoza kuwachitira chifundo<br />

koma sayamika, moti amalumanso dzanja limene<br />

likuwadyetsa. Munthu woti ndamupulumutsa,<br />

akufunanso kundiphera mwana!”<br />

Phunziro: Anthu oipa alibe pabwino.<br />

Mafunso<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

45


1. N’chifukwa chiyani munthu uja anatola Njoka?<br />

2. N’chifukwa chiyani Njokayo inkafuna kuluma<br />

mwana wa munthuyo?<br />

3. Kodi nkhaniyi ikusonyeza kuti munthuyo<br />

anaphunzirapo chiyani pa zimene zinachitikazo?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

46


Ntchentche Yosimbwa<br />

Kalelo kunali bambo wina wadazi. Bamboyo ankati<br />

akamaliza kudya nsima, ankakonda kukhala<br />

pakhonde kuti aphwetse mkhuto wake. Ndiye tsiku<br />

lina kunabwera Ntchentche n’kuyamba kumusokosa<br />

komanso kumuluma dazi lake. Kenako Ntchentcheyo<br />

inatera padazilo ndipo bamboyo anaganiza zoionetsa<br />

mbwadza poiphwanya ndi dzanja lake. Koma m’malo<br />

moti aphwanye ntchentcheyo, anamenya mutu wake,<br />

ndipo anamva ululu wosaneneka. Ntchentcheyo<br />

inapitirizabe kusimbwa, koma pa nthawiyi, nzeru<br />

zinamubwerera bamboyo moti sanalimbane nayo.<br />

Anati, “Umangodzivulaza wekha ukamalimbana ndi<br />

adani oipa.”<br />

Phunziro: Ukamalimbana ndi munthu woipa,<br />

umavutika ndi iweyo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

47


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani munthuyu anadzimenya<br />

m’mutu?<br />

2. N’chifukwa chiyani anaganiza zongosiya<br />

kulimbana ndi Ntchentcheyo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

48


Nkhandwe Ichezera Dokowe<br />

Kalekalelo Nkhandwe inali pa ubwenzi wa ponda apo<br />

m’pondepo ndi Dokowe. Ndiye tsiku lina Nkhandweyo<br />

inaitana Dokowe kuti akadye nkhomaliro kwawo.<br />

Koma Dokowe atafika, anapeza kuti wangomuphikira<br />

nsuzi ndipo anauika m’mbale yosalowa. Dokoweyo<br />

anayesetsa kuti amwe nsuziwo koma palibe chomwe<br />

anaphulapo. Nsuziwo unkangothera pamlomo wake<br />

wautali. Analimbana nawo kwa nthawi yaitali ndipo<br />

atatopa anangousiya, koma ali ndi njala kwambiri.<br />

Ndiye popeza paja amati, kwa eni kulibe mkuwo, mutu<br />

wa nkhuku n’chiwalo, dokowe sananene chilichonse.<br />

Anazindikira kuti mnzakeyo anachita izi pongofuna<br />

kumucheza basi. Kenako Nkhandwe inati, “Pepani kuti<br />

ndinakuphikirani nsuzi womwe simumaukonda.<br />

Ndikuona kuti udakali nde, mmene unalili.” Koma<br />

Dokowe anayankha kuti, “Usapepese ambwana,<br />

ndathokoza kwambiri chifukwa cha mtima wako<br />

wochereza alendo.” Kenako ananyamuka n’kuona<br />

msana wa njira. Ndiye tsiku lina, Dokowe nayenso<br />

anaitana mnzakeyu kuti akadye kwawo. Itangomva<br />

uthengawu, Nkhandweyo sinachedwechedwe, moti<br />

inauyamba ulendo wa kwa mnzakeyo. Itafika,<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

49


inamupeza akumudikirira ndipo inati, “Ndabwera<br />

bwanawe, paja okuluokulu odati kaitana kachita<br />

ujeni, ukachedwa ungakakapeze katabopha!”<br />

Mnzakeyo anaseka kwambiri ndipo kenako<br />

anamulowetsa m’nyumba kuti akadye zakudya<br />

zokoma zomwe anamukonzera. Zakudyazo anaziika<br />

mumtsuko wa kukamwa kwakung’ono, moti<br />

Nkhandwe sikadantha kulowetsa mutu wake n’kudya<br />

chakudyacho. Nkhandweyo inamva kuwawa mumtima<br />

mwake chifukwa cha zimenezi moti inangoyamba<br />

kunyambita kunja kwa mtsukowo. Ndiyeno Dokowe<br />

anati, “Sindipepesa ndi zimene zachitikazi, mwina<br />

ungaphunzirepo kathu. Nkhonya yobwezeratu<br />

imawawa?”<br />

Phunziro: Tizichitira ena zimene ifenso timafuna<br />

atatichitira.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

50


Mafunso<br />

1. Kodi Nkhandwe inachitira bwanji Dokowe<br />

chipongwe?<br />

2. Nanga Dokowe anachita chiyani atazindikira<br />

zimenezi?<br />

3. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani tinganene<br />

kuti Nkhandwe ndi Dokowe sanali mabwenzi a<br />

pamtimadi?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

51


Nkhandwe Itola Chigoba<br />

Tsiku lina Nkhandwe inalowa m’chipinda china<br />

chomwe anthu ochita zisudzo ankasungamo zinthu<br />

zawo. Mwadzidzidzi, Nkhandweyo inaona nkhope ya<br />

munthu ikumuyang’ana ndipo inayamba kuchita<br />

mantha. Koma itayang’anitsitsa bwinobwino inaona<br />

kuti chinali chigoba chomwe ochita zisudzo ankavala<br />

akamachita sewero. Ndiyeno Nkhandweyo inati, “Kani<br />

ndi iweyo? Umaonekatu ngati ndiwe munthu<br />

weniweni. Koma n’zomvetsa chisoni kuti ulibe<br />

ubongo.”<br />

Phunziro: Osamapusitsidwa ndi maonekedwe akunja.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkachita<br />

mantha itaona chigoba?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nkhandweyo inauza<br />

chigobacho kuti, “N’zomvetsa chisoni kuti ulibe<br />

ubongo”?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

52


Timba Atengeka Ndi Mbalame Zokongola<br />

Tsiku lina Timba anapita kukawongola miyendo<br />

kumalo amene mbalame zina zokongola kwambiri<br />

zotchedwa Pikoko zinkakonda kukhala, ndipo anatola<br />

nthenga zososoka za mbalamezo n’kuzimangirira<br />

kuchipsepse chake n’kumayenda moyerekedwa,<br />

kwinaku akulowera kumene kunali mbalamezo. Ndiye<br />

mbalamezo zitamuona, zinakwiya kwambiri moti<br />

zinamugwira n’kumuchotsa nthenga anamanga<br />

kuchipsepse zija. Chifukwa cha manyazi, Timbayo<br />

anabwerera kumene kunali mbalame zinzake, zomwe<br />

zinkaona zimene zinkachitikazo zili chapatali.<br />

Anzakewo anamukwiyira kwambiri ndipo anamuuza<br />

kuti, “Si kukongola kwa nthengatu kumene<br />

kumapangitsa mbalame kukhala yabwino, koma<br />

mtima.”<br />

Phunziro: Maonekedwe akunja sanena zambiri za<br />

mtima wa munthu.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

53


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani mbalame zokongola<br />

zinazula nthenga pa chipsepse cha Timba?<br />

2. N’chifukwa chiyani anzake a Timba<br />

anakhumudwa ndi zimene mnzawo anachitazi?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

54


Kudzitama Kunaphetsa Chule<br />

Tsiku lina Chule ndi bambo ake anakhala m’mbali<br />

mwa dziwe n’kumawothera dzuwa. Chuleyo anauza<br />

bambo ake kuti, “Bambo, dzulo ndinaona chinthu<br />

chachikulu koopsa. Chinalitu chachikulu, chachikulu<br />

zedi ngati phiri. Chinali ndi nyanga ziwiri zikuluzikulu<br />

pamutu pake, chimchira chachitali komanso<br />

dzimapazi zikuluzikulu.” Kenako bamboyo anati,<br />

“Takhala chete iwe, imene ukunenayotu ndi Ng’ombe<br />

ya mlimi wa pamtundapo. Koma sikuti ndi yaikulu<br />

mmene ikuneneramo, ukungokokomeza iwe!<br />

Yangokhala yaitaliko pang’ono poyerekeza ndi ineyo,<br />

moti nanenso nditadzifufumitsa ndikhoza kufanana<br />

nayo. Dikira uone . . . .” Kenako Chuleyo anakokera<br />

mpweya n’kudzifufumitsa kwambiri. Ndiyeno anafunsa<br />

mwana wakeyo kuti, “Kodi ng’ombeyo inali yaikulu<br />

chonchi?” Mwanayo anayankha kuti, “Ayi, inali<br />

yaikulu kuposa pamenepo.” Chuleyo anapitirizabe<br />

kukokera mpweya ndipo anadzifufumitsa,<br />

n’kudzifufumitsa kenako n’kudzifufumitsa. Ndiyeno<br />

anafunsa kuti, “Nanga bwanji pamenepo?” Mwanayo<br />

anayankhanso kuti, “Ayi, inali yaikulu, yaikulu<br />

kwambiri kuposa pamenepo.” Ndiyetu Chule<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

55


wamkuluyo anakoka mpweya, kuukoka, n’kuukoka<br />

moti anafufuma, kufufuma kenako n’kufufuma.<br />

Ndiyeno anati, “Ndikuganiza kuti Ng’ombeyo sinali<br />

yaikulu kuposa apa . . . ” Atangonena zimenezi, nthawi<br />

yomweyo anaphulika.<br />

Phunziro: Kufuna kuoneka wochenjera kumabweretsa<br />

mavuto.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani chule wamng’ono<br />

ankaganiza kuti waona chilombo chachikulu<br />

koopsa?<br />

2. Mukuganiza kuti n’chiyani chinachititsa kuti<br />

bambo a Chuleyo asonyeze mwana wakeyo kuti<br />

akhoza kufanana ndi chilombocho?<br />

3. N’chiyani chinapangitsa kuti bamboyo<br />

aphulike?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

56


Ubwenzi wa Mkango ndi Kapolo<br />

Tsiku lina kapolo wina anathawa kwawo n’kulowa<br />

m’nkhalango ina. Pamene ankayendayenda<br />

m’nkhalangomo anakumana ndi Mkango womwe<br />

unkabagula. Atangouona anatembenuka n’kuyamba<br />

kuthawa, koma anadabwa atazindikira kuti mkangowo<br />

sukumuthamangitsa. Kenako anaima n’kubwerera<br />

kumene kunali Mkango uja. Pamene ankauyandikira,<br />

mkangowo unamuonetsa dzanja lake lomwe<br />

linkatuluka magazi. Kapoloyo anaona minga yaikulu<br />

yomwe inabaya mwendo wa mkangowo ndipo<br />

unkamva ululu wosaneneka. Kapoloyo anamva chisoni<br />

kwambiri moti anachotsa mingayo n’kumangapo<br />

nsanza. Atangomaliza kuchita zimenezi, Mkangowo<br />

unadzuka n’kuyamba kunyambita kapoloyo ngati<br />

mmene amachitira galu. Kenako unatenga kapoloyo<br />

n’kupita naye kuphanga lake ndipo tsiku lililonse<br />

unkamubweretsera nyama yoti adye. Koma pasanapite<br />

nthawi, Mkangowo komanso kapoloyo anagwidwa ndi<br />

anthu a kumudzi anathawa kuja. Chifukwa choti<br />

kapoloyo anathawa mbuye wake anaweruzidwa kuti<br />

aphedwe pomusiya kuti adyedwe ndi mkango. Kenako<br />

anasiya Mkangowo osaupatsa chakudya kwa masiku<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

57


angapo kuti akadzangoumasura, udzapwepwete ndi<br />

mafupa omwe. Mfumu komanso anthu a m’mudzimo<br />

anasonkhana pabwalo lina kuti aone zimenezi<br />

zikuchitika ndipo asilikali anagwira kapolo uja<br />

n’kumapita naye kumene kunali Mkango kuja. Kenako<br />

asilikali anamasula chingwe chomwe anamangira<br />

Mkangowo ndipo unayamba kuthamanga ukubangula<br />

n’kumapita komwe kunali kapolo uja. Koma<br />

Mkangowo utayandikira, unazindikira kuti ndi bwenzi<br />

lake lomwe linamusamalira atavulala. Moti unagona<br />

pansi pafupi ndi kapoloyo n’kuyamba kunyambita<br />

manja ake monga mmene amachitira galu. Mfumu ya<br />

mudziwo inadabwa ndi zimenezi ndipo inaitanitsa<br />

kapoloyo. Kapoloyo anafotokoza zonse zomwe<br />

zinachitika ndipo Mfumuyo inakhululukira kapoloyo.<br />

Mkango ujanso unamasulidwa n’kupita kunkhalango.<br />

Phunziro: Ukamachitira ena zabwino, nawonso<br />

amadzakuthandiza zikadzakusokonekera.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

58


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani kapolo anathandiza<br />

Mkango?<br />

2. N’chiyani chinachititsa kuti Mkango ndi<br />

kapoloyo azigwirizana?<br />

3. Kodi mfumu inaphunzirapo chiyani pamene<br />

kapoloyo anafotokoza zimene zinachitika kuti<br />

Mkangowo usamudye?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

59


Mleme Uchenjera Pogona<br />

Pa nthawi ina, zilombo zakuthengo ndi mbalame<br />

zinayambana moti panakonzedwa zoti pachitike<br />

nkhondo. Ndiye mbalame zinayamba kusonkhanitsa<br />

asilikali ake, nazonso zilombo zinayamba kuchita<br />

chimodzimodzi. Koma Mleme unkakana kulowa ku<br />

gulu lililonse. Mbalame zinkati zikauuza kuti ukhale<br />

msilikali unkati: “Inetu ndili m’gulu la zilombo, siine<br />

mbalame.” Komanso zilombo zikauuza kuti, “Bwera<br />

udzalowe gulu lathu,” ankayankha kuti, “Inetu ndine<br />

mbalame, ndiye ndilowa bwanji m’gulu lanu?” Koma<br />

mwamwayi, nkhondo ija inalephereka ndipo mbalame<br />

komanso zilombo zakuthengo zinagwirizana<br />

zokhazikitsa mtendere. Kenako mbalame komanso<br />

zilombo zija zinakonza phwando lokondwerera kuti<br />

nkhondoyo yalephereka. Ndiye mleme unaganiza<br />

zokasangalala nawo ndipo unapita kumene kunali<br />

mbalame koma mbalame zonse zinagwanda. Kenako<br />

unauluka n’kupita kumene kunali zilombo<br />

zakuthengo. Koma nazonso zinamukana ndipo<br />

zinamuuza kuti akapanda kunyamuka zikuonetsa<br />

zakuda. Mlemewo unadandaula kwambiri ndi zimenezi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

60


ndipo unati, “Ukakhala kuti suli m’gulu lililonse,<br />

umakhala wekha.”<br />

Phunziro: Osamafuna anzathu pakakhala pamtendere.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Mleme unakana kukhala<br />

m’gulu la mbalame komanso la zinyama?<br />

2. N’chifukwa chiyani mbalame komanso zinyama<br />

zinakana Mleme atabwera kuti adzasangalale<br />

nawo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani pamenepa?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

61


Nkhani ya Mbawala ndi Mlenje<br />

Tsiku lina Mbawala inkamwa madzi ndipo inayamba<br />

kugomera chithunzithunzi chake chomwe<br />

chinkaoneka m’madzi. Kenako inati, “Ndi ndani<br />

winanso amene ali ndi nyanga zokongola chonchi<br />

m’nkhalango muno?” Kenako inayang’ana miyendo<br />

yake n’kunena kuti, “Ndimalakalaka ndikanakhala ndi<br />

miyendo yolongosoka yoti izigwirizana ndi nyanga<br />

zamtengo wapatali zomwe zili m’mutu mwangazi.<br />

Zimandiwawa kwambiri ndikaganizira kuti miyendo<br />

yanga ndi yoonda ngati zotokosera m’mano.” Mawu<br />

amenewa ali m’kamwa, kunatulukira mlenje ndipo<br />

anayamba kuithamangitsa. Koma chifukwa choti<br />

miyendo yake ndi yopepuka, Mbawalayo<br />

inangotsomphoka n’kuthawa, moti posapita nthawi<br />

inali patali kwambiri. Mbawalayo inapitirizabe<br />

kuthamanga ndipo inasiya kuyang’ana komwe<br />

imapita, moti inalowa m’ziyangoyango. Chifukwa cha<br />

kukula kwa nyanga zake, inakanirira<br />

m’ziyangoyangozo ndipo mlenje uja anaipeza<br />

n’kungoitola. Mbawalayo inayamba kulira ndipo<br />

mumtima mwake inkati, “N’chifukwa chiyani<br />

timakonda kunyoza zinthu zomwe zimatithandiza<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

62


kwambiri, n’kumakonda zinthu zomwe zikhoza kutiika<br />

m’mavuto?”<br />

Phunziro: Zinthu zimene zimaoneka zonyozeka<br />

m’zimene zimatithandiza kuti tikhale ndi moyo.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani mbawala inkafuna kukhala<br />

ndi miyendo yokongola?<br />

2. Kodi n’chiyani chinachititsa kuti Mbawala<br />

igwidwe?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

63


Njoka Ipsa Mtima<br />

Tsiku lina njoka inalowa m’nyumba ya munthu wina<br />

momwe munali zitsulo komanso zinthu zina.<br />

Ikuyenda, njokayo inayamba kukandidwa ndi chitsulo<br />

chinachake, moti inapsa mtima n’kuyamba<br />

kuchimenya. Itaona kuti palibe chimene chimachitika<br />

inangosiya kulimbana ndi chitsulocho n’kumapita.<br />

Inkaona kuti ikhoza kungotaya nthawi yake<br />

kumalimbana ndi chinthu chomwe sichimva<br />

kupweteka.<br />

Phunziro: N’kupanda nzeru kumalimbana ndi chinthu<br />

chomwe sichimva kupweteka.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi n’chifukwa chiyani njoka inayamba<br />

kumenya chitsulo?<br />

2. Kodi mungapereke chitsanzo cha zimene anthu<br />

amachita zomwe zimakhala ngati kulimbana ndi<br />

chitsulo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

64


Mitengo Inadzipweteketsa<br />

Tsiku lina munthu wina anapita kunkhalango<br />

nkhwangwa ili m’manja. Munthuyo ankapita<br />

kunkhalangoko kuti akapemphe nthambi ya mtengo<br />

woti aike kunkhwangwa yakeyo, ndipo anauza<br />

mitengo yomwe anaipeza m’nkhalangomo kuti<br />

imuchitire chifundo n’kumupatsa zomwe amafunazo.<br />

Mitengoyo itamva dandauloli, inafunsa munthuyo kuti<br />

akufuna akachite chiyani ndi nkhwangwayo akaika<br />

nthambiyo. Munthuyo anayankha kuti, “Ndikufuna<br />

ndikachitire zinthu zofunika kwambiri.” Popeza<br />

mitengo inali yachifundo, inapatsa munthuyo zomwe<br />

ankafuna. Kenako munthuyo anatenga mtengowo<br />

n’kuika kunkhwangwayo ndipo anayamba kugwetsa<br />

mitengo ya m’nkhalangomo. Mitengoyo itaona zimenezi<br />

inayamba kudandaula kuti sinaganize bwino popereka<br />

kwa mdani wawo chida choti awaphere.<br />

Phunziro: Osamapereka chida kwa mdani wako<br />

chifukwa akhoza kukuphera chomwecho.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

65


Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti mitengo sinkadziwa<br />

chimene munthuyo ankafuna kuchita ndi<br />

nkhwangwa yomwe inali m’manja mwake?<br />

2. Kodi mitengo ikanapewa bwanji mavuto amene<br />

anabwera pambuyo pake?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

66


Galu Akumana ndi Nkhandwe<br />

Nkhandwe inali itatheratu chifukwa cha njala pamene<br />

inakumana ndi Galu wina yemwe ankangodziyendera.<br />

Galuyo anati: “Oo! kodi ndi abwenzi? Inetu<br />

ndinkadziwa kuti moyo wanu wosakhazikikawu<br />

udzakubweretserani mavuto. Mufa ndi njalatu! Bwanji<br />

osamagwira ntchito ngati mmene ndimachitira ine kuti<br />

muzipatsidwa chakudya nthawi zonse?” Nkhandweyo<br />

inati, “Apo ndiye sindingakutsutse m’bale wanga.<br />

Ngati mwayi utapezeka ndikhoza kuchita zomwezo.”<br />

Kenako Galuyo anati, “Tiye tipite kwa abwana anga<br />

ndipo uzikagwira ntchito imene ndimagwira. Ngati<br />

utamakagwira ntchito molimbikira, ukhoza<br />

kudzakhala Nkhandwe yodya bwino.” Kenako nyama<br />

ziwirizi zinauyamba ulendo wopita kunyumba kwa<br />

galu. Koma zili m’njira, Nkhandwe inaona kuti pakhosi<br />

pa Galu panali poperepeseka ndipo inafunsa kuti,<br />

“Kodi khosi lakoli linatani bwanawe?” Galuyo<br />

anayankha kuti, “Aaa, ndi mmene lilili. Pamenepa<br />

m’pamene pamadutsa kolala. Pakolala imeneyo ndi<br />

pamene amakolekapo chingwe chomwe amandimanga<br />

nacho ndikamagwira ntchito usiku. Nthawi zina<br />

chimapana pakhosipa ndithu, n’chifukwa chake<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

67


ubweya wina wasosokapo. Koma aa ndi zazing’ono,<br />

ukazolowera monga mmene ndinachitira ineyo.”<br />

Kenako nkhandweyo inati, “Umenewotu ndi moyo<br />

wovuta, kwathu timakhala mwaufulu ife. Basi tionana,<br />

ndikupita kwathu ine.”<br />

Phunziro: Ndibwino kumaonda uli paufulu kusiyana<br />

ndi kumanenepa uli kapolo.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Galu ankafuna kuthandiza<br />

Nkhandwe?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inaganiza<br />

zokana mwayi wa ntchito womwe Galu<br />

anamupezera?<br />

3. Kodi pali nthano iliyonse yomwe munaimvapo,<br />

yomwe ikugwirizana ndi nkhaniyi?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

68


Ziwalo Ziukira Mimba<br />

Tsiku lina ziwalo za thupi zinakwiya kwambiri.<br />

Ziwalozi zinkaona kuti zimagwira ntchito yotopetsa,<br />

pomwe mimba imangokhala, koma n’kumadya<br />

zakudya zonse. Choncho zinachita msonkhano ndipo<br />

zitakambirana, zinagwirizana kuti zinyanyale ntchito.<br />

Zinanena kuti ziyambiranso pokhapokha mimba<br />

ikavomera kuti izigwira nawo ntchito. Ndiyeno kwa<br />

masiku angapo, mikono inkakana kunyamula<br />

chakudya kupititsa pakamwa. Nalonso kamwa<br />

linkakana kulandira chakudya. Zimenezi zinachititsa<br />

kuti mano azisowa ntchito yoti agwire. Kenako ntchito<br />

zonse zinaimiratu. Koma patatha masiku atatu, ziwalo<br />

zija zinayamba kufooka. Manja ankalephera kusuntha<br />

komanso miyendo inkalephera kuima. Pamapeto pake<br />

ziwalozo zinaona kuti nayonso mimba inkagwira<br />

ntchito yotamandika zedi, ngakhale inali yosaonekera.<br />

Zinaonanso kuti chiwalo chilichonse chimagwira<br />

ntchito yaikulu kuti zinthu ziziyenda bwino.<br />

Phunziro: Mgwirizano umathandiza kuti zinthu<br />

ziyende.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

69


Mafunso<br />

1. Kodi ziwalo zina zija zinkafuna kuti mimba<br />

izichita chiyani?<br />

2. Kodi zinachita chiyani pofuna kukakamiza<br />

mimba kuti nayonso izigwira ntchito?<br />

3. Kodi ziwalo zinazo zinaphunzirapo chiyani?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

70


Mlimi Agwira Gwape Atabisala<br />

Tsiku lina Mlenje ankathamangitsa Gwape ndipo<br />

anam’tengetsa kwambiri moti anangotsala pang’ono<br />

kumugwira. Koma Gwapeyo anathawa n’kukalowa<br />

m’nkhola la mlimi wina n’kudzikwirira ndi zakudya za<br />

Ng’ombe. Miyendo yake yokha ndi imene inkaonekera.<br />

Kenako Mlenje uja anafika pakhomo pa Mlimiyo ndipo<br />

anafunsa mwana wa pakhomopo kuti, “Kodi unaona<br />

Gwape atadutsa apa?” Mwanayo ananena kuti<br />

sanamuone ndipo anayang’anayang’ana m’nkhola<br />

komanso malo ena a pafupi koma sanamupeze.<br />

Ataona kuti zamuvuta, Mlenjeyo anaona msana wa<br />

njira. Kenako Mlimi yemwe anali mwini malowo<br />

anatulukira ndipo atayang’ana m’khola la ng’ombelo<br />

anaona kuti simukuoneka mmene mumaonekera<br />

nthawi zonse. Anayamba kuloza kumene kunali<br />

zakudya za Ng’ombe kuja n’kunena kuti, “Kodi<br />

mitengo ikuoneka pali zakudya za Ng’ombepo ndi ya<br />

chiyani?” Kenako mwana wake uja anapita pamene<br />

panali zakudyazo ndipo atakoka mitengoyo<br />

anangozindikira kuti akukoka Gwape.<br />

Phunziro: Chule anadabwa m’madzi muli mwake.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

71


Mafunso<br />

1. Kodi n’chiyani chinachititsa kuti Mlimiyu<br />

agwire Gwape?<br />

2. Kodi n’chifukwa chiyani mnyamata uja<br />

komanso Mlenje uja analephera kuona Gwapeyo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

72


Nkhandwe M’munda wa Mpesa<br />

Tsiku lina Nkhandwe inkayenda m’munda wina ndipo<br />

inafika pamalo ena pomwe panali zipatso za mpesa<br />

zomwe zinkaoneka kuti ndi zakupsa, koma kungoti<br />

zinali zitayanga pamtengo wautali. Itaona mphesazo,<br />

Nkhandweyo inati, “Ndidye mpesazi kuti ndiphe<br />

ludzu.” Kenako inabwerera m’mbuyo n’kudumpha,<br />

koma sinafike pamene panali mpesazo. Inabwereranso<br />

m’mbuyo koma inaphonyanso. Inachita zimenezi<br />

kambirimbiri, koma palibe chomwe inaphulapo.<br />

Kenako inatopa ndipo inanyamuka n’kumapita kwawo<br />

itaimika mphuno zake m’mwamba, kwinaku ikunena<br />

kuti, “Ndikuganiza kuti mphesa zimenezi ndi zowawa.”<br />

Phunziro: Zimakhala zosavuta kumanyoza zinthu<br />

zomwe zakukanika kuzipeza.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inasiya mpesa?<br />

Kodi tinganene kuti simazifuna?<br />

2. N’chifukwa chiyani nkhandweyo inanena kuti<br />

mphesazo zinali zowawa?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

73


Ikakuthawa Imawawa Msuzi<br />

Munthu wina anagwira Njiwa ndipo anasangalala<br />

kwambiri chifukwa ankadziwa kuti nsima ya tsiku<br />

limenelo ikayenda. Koma ali mkati moganiza zimenezi,<br />

Njiwayo inamupulumuka n’kuthawa. Munthuyo<br />

anapsa mtima n’kuyamba kuikuwira Njiwayo<br />

n’kumaiuza kuti, “Iweeeeeeeee, umawawa msuzi!”<br />

Phunziro: Osamanyoza chinthu chikapita.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi munthuyu ankaganiza zochita nayo<br />

chiyani Njiwa anagwirayo?<br />

2. N’chifukwa chiyani Njiwayo itamupulumuka<br />

anaikuwira n’kuiuza kuti imawawa nsuzi?<br />

3. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />

anthu amanyoza chinthu chikapita? Chimakhaladi<br />

kuti ndi choipa? Fotokozani.<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

74


Hatchi Akhaulitsa Mphoyo<br />

Kalekalelo Hatchi ndi Mphoyo zinayambana, ndiye<br />

Hatchi anapita kwa Mlenje n’kumupempha kuti<br />

amuthandize kukhaulitsa Mphoyo. Mlenjeyo<br />

anavomeradi, koma anati: “Ngati ukufunadi kuti<br />

ndikuthandize kukhaulitsa mdani wakoyu, uyenera<br />

kumvera zimene nditakuuze. Undilole kuti<br />

ndizikutsogolera komanso ndimangirire chingwe ichi<br />

pakamwa pako kuti ndikakwera pamsana pakopa<br />

ndizichigwira kuti ndisagwe. Komanso ndiike chishalo<br />

ichi pamsana pako n’cholinga choti ndisamamve<br />

kupweteka ndikakhalapo.” Hatchiyo inagwirizana ndi<br />

zimenezi ndipo Mlenjeyo anachitadi zomwe<br />

anapanganazo. Zitatero, mothandizidwa ndi Mlenjeyo,<br />

Hatchiyo inakhaulitsadi Mphoyo ija. Kenako Hatchi<br />

inauza Mlenjeyo kuti, “Popeza zimene timafuna<br />

zatheka, tsikatu pamsana pangapa komanso chotsa<br />

chingwe wandimanga pakamwachi. Chotsanso<br />

chishalo chili pamsanachi.” Koma Mlenjeyo anati,<br />

“Osathamanga magazi a Hatchi, ndikusangalala<br />

kwambiri kukhala pamwamba pano, moti uiwale zoti<br />

nditsikapo.”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

75


Phunziro: Ngati utavomera kuti anthu akugwiritse<br />

ntchito pokwaniritsa cholinga chako, nawonso<br />

amakugwiritsa ntchito pokwaniritsa cholinga chawo.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Hatchi inapita kwa Mlenje?<br />

2. N’chifukwa chiyani Mlenje anathandiza Hatchi?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

76


Mbalame Yadyera<br />

Tsiku lina mbalame ina yotchedwa Pikoko inapita kwa<br />

Mulungu kukapempha kuti aipatse mawu anthetemya<br />

oti azigwirizana ndi kukongola kwake. Mulunguyo<br />

atamva pempho la mbalameyi anakana kuichitira<br />

zimene inkafunazo. Koma mbalameyi inakakamirabe<br />

ndipo inauza mulunguyo kuti amuchitire zimene<br />

amafunazo basi. Pofuna kukakamiza Mulunguyo kuti<br />

achite zimene inkafunazo, mbalameyi inauza<br />

Mulunguyo kuti amuchitire chifundo chifukwa<br />

m’mbuyomo mulunguyo anali atanenapo kuti<br />

mbalameyo ndi yokongola komanso yokondedwa<br />

kwambiri kuposa mbalame zonse. Koma Mulunguyo<br />

anaiuza mbalameyo kuti, “Uzikhutira ndi zimene uli<br />

nazo. Sungakwanitse kupeza chilichonse chimene<br />

ukufuna, komanso sungakhale katswiri pa<br />

chilichonse. Kusayamika bwanji, kukongolako<br />

sikumakukwanira?”<br />

Phunziro: Palibe munthu amene amadziwa zonse.<br />

Palibe munthu amene amakhala katswiri pa<br />

chilichonse.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

77


Mafunso<br />

1. Kodi mbalameyi inkafuna kuti Mulungu<br />

aichitire chiyani?<br />

2. N’chifukwa chiyani Mulungu anakana?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

78


Chizolowezi Chimabala Mwano<br />

Nkhandwe ina inamva zoti Mkango ndi woopsa<br />

kwambiri komanso kuti ndi Mfumu ya Nyama zonse.<br />

Ulendo woyamba umene Nkhandweyi inakumana<br />

nawo, inachita mantha kwambiri moti inaliyatsa liwiro<br />

n’kukabisala m’nkhalango. Koma itakumananso ndi<br />

Mkangowo ulendo wachiwiri, inaima patali<br />

n’kumauyang’ana ukudutsa. Koma kenako inatha<br />

mantha, ndipo itakumana nawonso ulendo wachitatu,<br />

inayamba kuyenda n’kumapita kumene kunali<br />

Mkangowo ndipo inaufunsa kuti mkazi ndi ana ake ali<br />

bwanji. Inafunsaso Mkangowo kuti, “Kodi<br />

tidzakumananso liti?” Kenako inatembenuka<br />

n’kumapita, kwinaku ikuyendetsa mchira wake<br />

mwamwano.<br />

Phunziro: Ukazolowerana ndi munthu umasiya<br />

kumulemekeza.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

79


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inachita mantha<br />

itakumana koyamba ndi Mkango?<br />

2. Kodi Nkhandwe inkachitanso mantha<br />

itakumana ndi Mkango ulendo wachitatu?<br />

N’chifukwa chiyani sinkachita mantha? Kodi<br />

Mkangowo unali utasintha?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

80


Munthu Atsutsana ndi Mkango<br />

Tsiku lina Munthu ndi Mkango ankakambirana kuti<br />

wamphamvu ndi ndani pakati pawo. Munthuyo<br />

ankanena kuti anthu ndi amphamvu kwambiri kuposa<br />

Mikango chifukwa ali ndi nzeru zambiri. Ndiyeno<br />

Munthuyo anauza Mkangowo kuti, “Tabwera kuno<br />

ndikuonetse chinthu chinachake kuti umvetse zoti<br />

anthu ali ndi mphamvu zoopsa.” Kenako anatengana<br />

ndi Mkangowo n’kupita nawo pamalo ena, ndipo<br />

anauonetsa chipilala cha Samisoni akukhadzula<br />

kamwa la Mkango ndi manja. Kenako Mkangowo<br />

unati, “Chabwino, koma zimene wandionetsazi si<br />

umboni woti anthu ndi amphamvu kuposa Mikango.<br />

Si, anthu ndi amene anapanga chipilalachi?”<br />

Phunziro: Munthu akhoza kukhotetsa nkhani kuti<br />

igwirizane ndi maganizo ake.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

81


Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />

chipilala chinkasonyeza kuti Munthu ndi<br />

wamphamvu kuposa Mkango?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti Mkango ukanapanga<br />

chipilalacho, chikanakhala chosiyana ndi<br />

chimenechi? Nanga bwenzi chikuoneka bwanji?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

82


Nyerere Yanzeru<br />

Tsiku lina Chiwala chinkadumphadumpha, muluzi uli<br />

pakamwa ndipo chinkaoneka kuti sichikudandaula<br />

chilichonse. Kenako Nyerere inadutsa itanyamula<br />

thumba la chakudya ndipo inali ili thukuta<br />

kamukamu. Nyerereyi inkagwira ntchito yolemetsayi<br />

chifukwa inkafuna kuti isunge chakudya chambiri<br />

kuphanga lake kuti mvula ikadzayamba kugwa<br />

isadzavutike. Ndiye Chiwala chinafunsa nyerereyo<br />

kuti, “Bwanji osabwera kuti tidzacheze,<br />

ukudzizunziranji chotere ngati kapolo? Sunamvepo<br />

mwambi wakuti, papsa tonola sudziwa mtima<br />

wamoto? Ndani akudziwa ngati mawa tidzukenso?”<br />

Nyerereyo inayankha kuti, “Ndikusonkhanitsa<br />

chakudya choti ndidzadye mvula ikadzayamba.<br />

Nawensotu ungachite bwino kuchitiratu zimenezi<br />

nthawi ikadalipo.” Ndiyeno Chiwalacho chinayankha<br />

mwamwano kuti, “Ndivutikirenji kusunga chakudya<br />

choti ndidzadye mvula ikadzayamba, pomwe panopa<br />

chakudya chilipo kutapa kutaya!” Itamva zimenezi,<br />

Nyerereyo sidayankhe, inangopitirizabe kututira<br />

chakudya kuphanga lake. Pamene mvula inkayamba<br />

Chiwala chinalibe kalikonse ndipo pakhomo pake<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

83


panali galu wakuda. Chiwalacho chinkasirira chikaona<br />

Nyerere ikugawana chakudya ndi ana ake ndipo<br />

chinati, “Ukakhala ndi zambiri, ndi bwino kumasunga<br />

zina zoti udzagwiritse ntchito zikadzakuvuta.”<br />

Phunziro: Ukakhala ndi zochuluka kumasungako zina<br />

kuti udzagwiritse ntchito ukadzakumana ndi mavuto.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Nyerere inauza Chiwala<br />

kuti chisunge chakudya choti idzagwiritse ntchito<br />

m’nthawi yamvula?<br />

2. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

84


Mtengo ndi Bango<br />

Tsiku lina Mtengo unauza Bango lomwe linamera<br />

pafupi ndi phazi lake kuti, “Mwana iwe, n’chifukwa<br />

chiyani suzika kwambiri mizu yako n’kuimika mutu<br />

wako m’mwamba ngati mmene ndimachitira ine?”<br />

Bangolo linayankha kuti, “Ayi, ndimakhutira ndi<br />

mmene ndilili komanso zomwe ndimakwanitsa<br />

kuchita. Mwina ndimaoneka wofooka, koma ndimaona<br />

kuti ndimatetezeka mwa njira imeneyi.” Mtengo<br />

utamva zimenezi, nkhope yake inachita tsinya ndipo<br />

unati, “Umatetezeka? Iweyotu ndi woonda kwambiri<br />

moti umangokhala ngati uli ndi matenda a<br />

kaliondeonde, kathupi kako kamangoti<br />

lobodolobodooo. Mphepo ikamawomba umangoti<br />

tepatepa. Komansotu ndiwe wosavuta kuzula. Koma<br />

taona ifeyo, amunamuna ogona kukhomo kosatseka.<br />

Ndani angalimbe mtima kuti andizule ndi mitsitsi<br />

yomwe? Komanso ndi ndani amene angalimbe mtima<br />

kuweramitsa mutu wanga pansi?” Mawu amenewa ali<br />

m’kamwa, kunabwera chimphepo champhamvu ndipo<br />

mphepoyo inazula Mtengo uja ndi mitsitsi yomwe moti<br />

Mtengowo unangoti lambaaa, mutu utaloza pansi.<br />

Koma Bango lija linangopindikira kumene kumalowera<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

85


mphepo ndipo mphepoyo itadutsa, linadzukanso<br />

n’kukhala tsonga. Kenako linafunsa Mtengo uja kuti,<br />

“Waona, tsopano wamphamvu ndi ndani?”<br />

Phunziro: Osamadzitama.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Mtengo unauza Bango zinthu zotani?<br />

2. N’chifukwa chiyani Bango linkaona kuti ndi<br />

lotetezeka?<br />

3. Kodi mukuganiza kuti kudzitama<br />

kumabweretsa mavuto otani?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

86


Nkhandwe Yatulo<br />

Tsiku lina Nkhandwe inkacheza ndi Mphaka ndipo<br />

inayamba kudzitama n’kumanena kuti imadziwa<br />

kuzemba komanso kuthawa adani ake. Inati:<br />

“Sungakhulupirire, mwina ndingonena kuti ndili ndi<br />

kathumba kosatsegula ka njira zosiyanasiyana zomwe<br />

ndikhoza kugwiritsa ntchito pothawa adani anga.<br />

M’thumba limenelo muli njira zoposa 100 zomwe<br />

ndikhoza kusankha imene ndikufuna kugwiritsa<br />

ntchito.” Koma Mphaka anati, “Ineyo ndili ndi njira<br />

imodzi basi, komabe imandipulumutsa adani anga<br />

akamandithamangitsa.” Nthawi yomweyo panayamba<br />

kumveka phokoso la agalu ndipo linkamveka kuti<br />

likubwera kumene kunali Nkhandwe ndi Mphaka<br />

kuja. Mphaka atamva phokosolo, nthawi yomweyo<br />

anathawira mumtengo n’kukabisala, ndipo anauza<br />

Nkhandweyo kuti, “Ine ndimagwiritsa ntchito njira<br />

imeneyi. Nanga iweyo ugwiritsa ntchito njira iti?”<br />

Kenako Nkhandweyo inayamba kuganizira za njira<br />

yoyamba n’kuona kuti sikugwira. Inaganizira za njira<br />

ina n’kuonanso kuti sikugwira. Inapitirizabe<br />

kuganizira njira zina ndipo pa nthawiyi agalu aja anali<br />

akuyandikira. Kenako Nkhandweyo inasokonezeka<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

87


ndipo agaluwo anaigwira moti mwini agaluwo anaipha.<br />

Pamene zimenezi zinkachitika, mphaka uja<br />

ankangoonerera ndipo anati, “Bola kukhala ndi njira<br />

imodzi yothandiza, kusiyana ndi kukhala ndi njira<br />

zambirimbiri zomwe ukungoganiza kuti zikhoza<br />

kukuthandiza.”<br />

Phunziro: Ndi bwino kukhala ndi chinthu chimodzi<br />

chothandiza, kusiyana ndi kukhala ndi zambiri zomwe<br />

sizingakuthandize.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Nkhandwe inauza Mphaka chiyani?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inalephera<br />

kuthawa agalu?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

88


Mmbulu Inavala Chikopa cha Nkhosa<br />

Pa nthawi ina, Mmbulu unkakhaula ndi njala<br />

chifukwa zinali zovuta kuba Nkhosa. M’busa wa<br />

Nkhosazo anali watcheru kwambiri komanso anali ndi<br />

galu woopsa yemwe sankanyengerera akaona nyama<br />

ina ikuyandikira Nkhosa. Koma tsiku lina, Mmbuluwo<br />

unatola chikopa cha Nkhosa chomwe chinatayidwa,<br />

ndipo inavala chikopacho n’kulowa m’gulu la Nkhosa<br />

zija. Choncho mkazi wa Nkhosa yomwe inaphedwayo,<br />

anayamba kuchita chidwi ndi Mmbuluwo<br />

n’kumaganiza kuti ndi mwamuna wake. Ndiyeno<br />

Mmbuluwo unayamba kulowera kwina, kuchoka pa<br />

gulu la Nkhosalo ndipo Nkhosa yaikaziyo<br />

inkangotsatira. Kenako Mmbuluwo unagwira<br />

Nkhosayo n’kuidya. M’kupita kwa nthawi unazolowera<br />

kuba nkhosa mwa njira imeneyi, moti inadya nkhosa<br />

zambiri m’busa komanso galu uja osadziwa.<br />

Phunziro: Maonekedwe amapusitsa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

89


Mafunso<br />

1. Kodi Mmbulu unapusitsa bwanji Nkhosa?<br />

2. N’chiyani chinachititsa kuti Nkhosa yaikazi ija<br />

iganize kuti Mmbuluwo ndi mwamuna wake?<br />

3. Mungapereke zitsanzo cha zinthu zina zomwe<br />

zimaoneka ngati ndi zabwino koma zili zoopsa?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

90


Galu Apezeka Modyera Ng’ombe<br />

Tsiku lina Galu anatopa kwambiri ndipo ankafuna<br />

atabako tulo. Ndiye anakalowa m’khola la Ng’ombe<br />

n’kudziponya pamene panali zakudya za ng’ombezo.<br />

Pasanapite nthawi, Galuyo anayamba kuliza<br />

mkonono. Koma pa nthawiyi m’pamene Ng’ombe<br />

inatulukira ili ndi njala zedi ndipo sinachedwenso,<br />

koma kupita pamene panali zakudya zake. Ng’ombeyo<br />

inadzutsa Galu uja n’kumusokonezera maloto ake<br />

okoma. Galuyo anapsa mtima ndi zimenezi ndipo<br />

anayamba kuuwa, wuuuuuuuuu! Uwuuuuu!<br />

Ng’ombeyo imati ikati iyandikire zakudya zakezo,<br />

Galuyo ankauwa kwambiri ndipo ankafuna kuiluma.<br />

Kenako Ng’ombeyo inangomusiya ndipo inanyamuka<br />

n’kumapita kwinaku ikung’ung’udza kuti, “Aa, anthu<br />

ena amakonda kulusira anzawo pa zinthu zomwe<br />

sizingawathandize n’komwe.”<br />

Phunziro: Anthu ena amayambana ndi anzawo pofuna<br />

kuteteza zinthu zomwe sangazigwiritse ntchito<br />

komanso sizingawathandize.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

91


Mafunso<br />

1. Kodi Galu ankagwiritsa ntchito bwanji zakudya<br />

za Ng’ombe zija?<br />

2. N’chifukwa chiyani Ng’ombe inapita pamene<br />

Galu uja anagona?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

92


Fano Lathabwa<br />

Kalekalelo, anthu ena ankalambira miyala komanso<br />

mafano. Ankapempha milungu yawoyi kuti iwadalitse<br />

komanso iwathandize kupeza zimene akufuna pamoyo<br />

wawo. Koma panali munthu wina yemwe anali<br />

kwakwatuke wotheratu. Munthuyu ankapempha<br />

mulungu wake wathabwa kuti amuthandize, koma<br />

palibe chimene chinkachitika. Bambo ake ndi amene<br />

anamupatsa fanolo ngati cholowa. Munthuyu<br />

samatopa kupempha mulungu wakeyo kuti amupatse<br />

mwayi. Anachita zimenezi kambirimbiri, koma<br />

zinkangokhala ngati akulimbana ndi mtunda wopanda<br />

madzi. Tsiku lina, munthuyo anapsa mtima ndi<br />

mulungu wakeyo ndipo anamumenya mwamphamvu<br />

ndi chibakera ndipo mulunguyo anagwa pansi<br />

n’kusweka. Mkati mwa mulunguyo munatuluka<br />

ndalama zambirimbiri ndipo zinangoti mbweee<br />

m’nyumbamo. Munthuyo anangogwira pakamwa<br />

chifukwa chosowa chonena, ndipo anazindikira kuti<br />

bambo ake ndi amene anaika ndalamazo mkati mwa<br />

fanolo.<br />

Phunziro: Kulambira mafano kapena zinthu zina<br />

n’kosathandiza chifukwa zilibe moyo. Sizingakuuze<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

93


ngakhale zitakhala kuti munthu wina wabisa chuma<br />

mkati mwake. Lemba la Yesaya 44:14-17 limati: Pali<br />

munthu amene ntchito yake ndi yogwetsa mitengo ya<br />

mkungudza. Iye amasankha mtengo wamtundu<br />

winawake, waukulu kwambiri, n’kuusiya kuti ukule<br />

n’kukhwima pakati pa mitengo ya m’nkhalango. Iye<br />

anabzala mtengo wa paini, ndipo mvula yaukulitsa<br />

kwambiri. Tsopano mtengowo wafika poti munthu<br />

akhoza kuusandutsa nkhuni. Chotero iye watenga<br />

mbali ya mtengowo kuti asonkhere moto woti aziwotha.<br />

Wayatsa motowo n’kuphikapo mkate. Wasemanso<br />

mulungu woti azimugwadira. Mtengowo waupanga<br />

chifaniziro chosema ndipo akuchigwadira<br />

n’kumachilambira. Hafu ya mtengowo waitentha<br />

pamoto. Hafu ina ya mtengowo wawotchera nyama<br />

imene wadya, ndipo wakhuta. Wawothanso moto wake<br />

ndipo wanena kuti: “Eya! Ndafundidwa. Ndaona<br />

kuwala kwa moto.” Koma mtengo wotsalawo<br />

wapangira mulungu, wapangira chifaniziro chake<br />

chosema. Wachiweramira ndi kuchigwadira<br />

n’kumapemphera pamaso pake kuti: “Ndipulumutseni,<br />

pakuti ndinu mulungu wanga.” Munthu ameneyutu ndi<br />

wachaba. Chinthu wapanga yekhacho!<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

94


Mafunso<br />

1. Kodi munthuyo ankafuna kuti mulungu<br />

wakeyo amuchitire chiyani?<br />

2. N’chifukwa chiyani munthuyo anapsa mtima?<br />

3. Kodi tinganene kuti mulungu wakeyo<br />

anamuthandizadi?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

95


Msodzi<br />

Tsiku lina Msodzi anatenga chitoliro chake komanso<br />

ukonde wake n’kupita kumtsinje kuti akagwire<br />

nsomba. Atafika kumeneko, anapemphera kuti<br />

nsomba zibwere pamene anaika ukonde wakewo,<br />

koma palibe inabwera kapena kuonetsa mphuno yake<br />

pamwamba pa madzi. Kenako Msodziyo anakokera<br />

ukonde wakeyo chakumtunda ndipo<br />

anapempheranso. Mwadzidzidzi anangoona kuti mu<br />

ukondewo nsomba zayamba kuyenda pamwamba pa<br />

madzi komanso zina zikuphiriphitha, ndipo anati, “Aa,<br />

mwayamba kuvina ine ndikupemphera?” Ndiye<br />

nsomba yokalamba pa zonsezo inati, “Ukagwidwa ndi<br />

munthu wamphamvu, umafunika kumachita zimene<br />

akufuna.”<br />

Phunziro: Osamachita masewera ndi anthu<br />

amphamvu.<br />

Mafunso<br />

1. Msodziyo atagwira nsomba zija ndi ukonde<br />

wake, n’chifukwa chiyani nsomba zinayamba<br />

kuchita zimene msodziyo ankafuna? N’chifukwa<br />

chiyani mukutero?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

96


2. Kodi nsombazo zinkafunadi kuvina?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

97


Mnyamata Wabodza<br />

Kalekalelo kunali mnyamata wina yemwe ankaweta<br />

nkhosa yekhayekha pafupi ndi nkhalango ina<br />

yowirira. Mnyamatayu ankasowa wocheza naye ndipo<br />

ankangokhala yekhayekha tsiku lonse. Ndiye tsiku<br />

lina anapeza nzeru yomuthandiza kuti azisangalalako<br />

komanso kuti anthu azibwera n’kukhala naye pafupi.<br />

Anathamanga kumalowera kumene kunali mudzi<br />

wakwawo kwinaku akukuwa kuti, “Kuli Mikango, kuli<br />

Mikango kunoooooooooo!” Ndiye anthu a m’mudzimo<br />

anathamanga kudzakumana naye ndipo ena a iwo<br />

anaima limodzi naye kwa kanthawi<br />

n’kumamuyankhulitsa, moti panthawiyi<br />

sankasungulumwanso. Zimenezi zinamusangalatsa<br />

kwambiri, moti patapita masiku angapo, anachitanso<br />

chimodzimodzi. Ulendo umenewunso anthu a m’mudzi<br />

uja anabwera ndipo anakhala naye limodzi kwa<br />

nthawi yaitali ndipo mnyamatayo anasangalalanso<br />

kwabasi. Kenako anadzachitanso chimodzimodzi ndipo<br />

anthu a m’mudzi uja anatopa naye ndipo<br />

anam’tulukira kuti akungowapusitsa. Koma tsiku lina<br />

Mikango inatulukadi m’nkhalango ija ndipo inayamba<br />

kugwira Nkhosa zake. Mnyamatayo anayambanso<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

98


kukuwa kuti, “Kuli Mikango, kuli Mikango<br />

kunoooooooooo!” Anakuwa kwambiri kuposa<br />

poyamba, koma palibe anabwera. Anthuwo<br />

ankaganiza kuti mnyamatayo akungowanamiza ngati<br />

mmene anachitira maulendo ena aja. Mikangoyo<br />

inadya Nkhosa zambiri ndithu, ndipo itakhuta<br />

inabwerera m’nkhalango muja. Mnyamatayo<br />

anabwerera kumudzi kuja kwinaku akulira ndipo<br />

atafotokoza zimene zinachitika. Ndiyeno munthu wina<br />

wachikulire anamuuza kuti, “Anthu sakhulupirira<br />

munthu wabodza, ngakhale atakhala kuti akunena<br />

zoona.”<br />

Phunziro: Ukamanama anthu amakuzolowera, moti<br />

tsiku lina ukamadzanena zoona,<br />

samakukhulupiriranso.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

99


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani mnyamatayu ananena<br />

bodza?<br />

2. Kodi ndi mavuto ena ati amene akanabwera<br />

chifukwa cha bodza la mnyamatayu? Kodi<br />

tinganene kuti moyo wake unali pangozi?<br />

3. N’chifukwa chiyani anthu a m’mudzi uja<br />

sanakhulupirire ulendo womaliza womwe<br />

mnyamatayu ananena kuti kukubwera Mikango?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

100


Mpikisano wa Pakati pa Dzuwa ndi Mphepo<br />

Tsiku lina Mphepo komanso Dzuwa zinkatsutsana<br />

kuti wamphamvu ndi ndani pakati pawo. Mphepo<br />

inauza mnzakeyo kuti, “Inetu ndi wamphamvu zedi,<br />

ndimatha kuyalula denga la nyumba, kuzula mitengo<br />

komanso kugwetsa zinthu zikuluzikulu. Nditati<br />

ndifotokoze zonse zimene ndimachita, iweyo ukhoza<br />

kukalowa n’kutuluka, kenako n’kukalowanso.” Pa<br />

nthawiyi Dzuwa linkangomvetsera zimene mnzakeyo<br />

ankanena. Kenako anaona munthu akudutsa<br />

chapafupi, atavala chipewa. Ndiye Dzuwa linati,<br />

“Eyaaa, ndadziwa chochita tsopano. Kuti tidziwedi<br />

amene ali wamphamvu, tiye tipikisane. Tione amene<br />

angapangitse kuti munthuyo achotse chipewa<br />

chimene wavalacho.” Nthawi yomweyo Mphepo<br />

inasangalala ndipo inati, “Taulutsa zinthuzinthu ife,<br />

ndiye pali chiyani apaaa?” Kenako anagwirizana kuti<br />

iyambe Mphepo kuulutsa chipewacho. Koma Mphepo<br />

imati ikafuna kuulutsa chipewacho, munthuyo<br />

ankangochigwira n’kuchikhazikanso bwinobwino.<br />

Munthuyo ataona kuti Mphepo ikumuvutitsa,<br />

anangomanga chipewacho kuchibwano chake ndi<br />

chigwe. Mphepo inayesa kuulutsa chipewacho koma<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

101


inakanika ndipo inatopa kwambiri n’kukhala pansi<br />

kuti ipume. Kenako Dzuwa linalowa m’bwalo. Ndiye<br />

linaomba, n’kuomba ndipo kunja kunatentha zedi.<br />

Zitatero munthu uja anamva kutentha kwambiri ndipo<br />

anamasura chingwe chija n’kuvula chipewa chija.<br />

Kenako anakaima pamthunzi kuti mutu wake<br />

upitidwe mphepo.<br />

Phunziro: Osamadzitama, mwamuna mnzako ndi<br />

pachulu.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Mphepo inkaderera<br />

mphamvu za Dzuwa?<br />

2. Kodi tinganene kuti n’kulakwa kumadzitama?<br />

3. Kodi pamapeto pake ndi ndani amene<br />

anapambana?<br />

4. N’chifukwa chiyani Mphepo inalephera<br />

kuulutsa chipewa cha munthu uja?<br />

5. Kodi mukuganiza kuti Dzuwa likuimira<br />

chiyani?<br />

6. Nanga tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

102


Mnyamata wa Zala Zazitali<br />

Mnyamata wina anagwidwa ataba ndalama zambiri<br />

ndipo pofuna kuti ena atengerepo phunziro, mfumu ya<br />

m’deralo inalamula kuti aphedwe. Tsiku loti aphedwe<br />

litafika, mnyamatayo anapempha anthu omwe<br />

ankafuna kumupachikawo kuti amulole kuchita<br />

chinthu chimodzi asanaphedwe. Anapempha kuti<br />

akufuna auze mayi ake zinazake. Anthuwo<br />

anavomera, ndipo mnyamatayo anapita pafupi ndi<br />

mayi akewo n’kuwauza kuti, “Ndikufuna<br />

ndikunong’onezeni.” Mayiyo anaperekeradi khutu lake<br />

kuti mwana wakeyo amunong’oneze, koma mwanayo<br />

analuma khutulo ndipo linangotsala pang’ono<br />

kudukiratu. Anthu onse omwe anabwera<br />

kudzaonerera kuphedwa kwa mwanayo anadabwa ndi<br />

zimenezi ndipo ena ankati mchitidwe umenewu unali<br />

wankhanza zedi. Enanso ankanena kuti munthu<br />

wabwinobwino sangachite zomwe mnyamatayo<br />

anachita. Koma mnyamatayo anati: “Ndachita<br />

zimenezi kuti ndiwakhaulitse. Kungoyambira ndili<br />

mwana ndinkaba zinthu, koma ndikapita kunyumba,<br />

mayiwa ankalandira n’kusunga. M’malo moti<br />

andilangize kapena kundipatsa chilango, ankaseka<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

103


n’kunena kuti ‘palibe atadziwe zimenezi.’ Lero<br />

ndiphedwa chifukwa cha iwowa.” Atamva zimenezi,<br />

munthu wina wokonda kupemphera yemwe anali<br />

pamalopo anauza mayiyo kuti, “Mwanayu akunena<br />

zoona. Wafika pamenepa chifukwa inuyo<br />

munamulekerera. Pajatu amati, ‘Langiza mwana<br />

poyamba m’njira yake, ndipo ngakhale akadzakula<br />

sadzachokamo.’”<br />

Phunziro: Kumalangiza komanso kuphunzitsa ana<br />

adakali aang’ono.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mayiwa akanathandiza bwanji mwanayu<br />

ali wamng’ono?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti chinkapangitsa mayiyu<br />

kusapatsa mwana wakeyu chilango chinali<br />

chiyani?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

104


Bambo Yemwe Anakwatira Mitala<br />

Kalekalelo, amuna akuloledwa kukwatira akazi ambiri,<br />

bambo wina anakwatira akazi awiri. Wina anali<br />

wamkulu kwambiri kuposa msinkhu wake, ndipo<br />

winayo anali mtsikana. Akazi onsewa ankamukonda<br />

kwambiri ndipo aliyense ankafuna kuti mwamunayo<br />

azioneka mofanana naye. Wamkulu ankafuna kuti<br />

mwamunayo azioneka wachikulire, pomwe wamng’ono<br />

ankafuna azioneka wachinyamata. Ndiye n’kupita kwa<br />

nthawi, mwamuna uja anayamba kukalamba ndipo<br />

tsitsi lake linayamba kuyera. Mkazi wachitsikana uja<br />

anayamba kudana ndi tsitsi la imvilo chifukwa<br />

linkapangitsa kuti azioneka ngati anakwatiwa ndi<br />

mwamuna wamkulu kwambiri, ndipo ankaona kuti<br />

anthu azisokoneza n’kumaganiza kuti ndi bambo ake.<br />

Choncho tsiku lililonse mwamunayo akamagona,<br />

mkaziyo ankapesa tsitsi la mwamunayo n’kuthothola<br />

tsitsi lonse loyera. Koma mkazi wamkulu uja<br />

ankasangalala akaona kuti mwamuna wake wayamba<br />

kuchita imvi ndipo ankaona kuti zimenezi zithandiza<br />

anthu kuti asamaganize zoti mwamuna wakeyo ndi<br />

mwana wake. Choncho m’mawa ulionse mwamunayo<br />

asanadzuke, mkazi wamkuluyo ankathothola tsitsi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

105


lakuda lomwe linali m’mutu mwa mwamuna wakeyo.<br />

Pamapeto pake, tsitsi lonse la mwamunayo linatha<br />

ndipo anasanduka wadazi.<br />

Phunziro: Ukamangomvera aliyense, umasanduka<br />

chitsiru.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani mkazi wamkulu<br />

ankasangalala mwamuna wake atayamba imvi?<br />

2. Nanga n’chifukwa chiyani mkazi wamng’ono<br />

ankadana nazo?<br />

3. Kodi bamboyu anakumana ndi mavuto otani?<br />

4. Kodi n’zotheka kukhala wokalamba komanso<br />

wachinyamata nthawi imodzi?<br />

5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

106


Mayi ndi Nkhandwe<br />

“Ndati utontholeee!” Mawu amenewa anayankhula ndi<br />

Mayi wina ataima pazenera lotsegula. M’manja mwake<br />

munali mwana yemwe ankalira mosatonthozeka.<br />

Kenako mwanayo anatonthola ndipo Mayiyo<br />

anachenjeza mwanayo kuti, “Ukayambiranso kulira,<br />

ndikuponyera pazenerapa kuti Nkhandwe ikudye.”<br />

Ndiye zinangochitika kuti pa nthawi imene ankanena<br />

zimenezi, Nkhandwe inali ikudutsa chapafupi ndipo<br />

inamva zomwe mayiyo ananena. Nkhandweyo inaima<br />

pafupi ndi nyumbayo ndipo inayamba kudikira kuti<br />

mwanayo alirenso. Inati, “Lerotu ndiye ndachita<br />

mwayi. Ndikuganiza kuti alira posachedwapa, ana<br />

amakoma kwabasi moti nditsukako m’kamwa lero.”<br />

Nkhandweyo inadikira kwa nthawi yaitali, koma<br />

mwanayo sanalire. Kenako mwana uja anayambiranso<br />

kulira ndipo Nkhandweyo inaima pafupi ndi zenera lija<br />

kwinaku ikugwedezera mchira n’kumadikira kuti<br />

mayiyo aponye mwanayo pawindopo. Koma mayiyo<br />

anangotseka zeneraro n’kuyamba kumuyamwitsa.<br />

Posakhalitsa agalu a pakhomopo anatulukira n’kupeza<br />

Nkhandweyo ili pafupi ndi zeneraro ndipo<br />

Nkhandweyo inayamba kuthawa kwinaku ikunena<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

107


kuti, “Anthu ndi osathandiza, n’chifukwa chiyani<br />

nthawi zonse amapereka malonjezo akudziwa kuti<br />

sawakwaniritsa?”<br />

Phunziro: Anthu ambiri amalonjeza akudziwa kuti<br />

sakwaniritsa malonjezowo.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Mayiyu ankafunadi kutaya mwanayo<br />

pazenera?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inakhulupirira<br />

zimene Mayiyo ananena?<br />

3. N’chifukwa chiyani tinganene kuti sikuti panali<br />

ubwenzi uliwonse pakati pa Mayiyo ndi<br />

Nkhandwe?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

108


Msamuko wa Kamba<br />

Tsiku lina Kamba, kapena kuti Fulu, anapeza malo<br />

atsopano ndipo ankafuna kusamukira kumalowo.<br />

Ndiye anapempha mbalame ina yotchedwa Nkhwazi<br />

kuti imunyamule n’kukamusiya kumalowo ndipo<br />

analonjeza kuti aifumbatitsa kenakake. Nkhwaziyo<br />

inavomera ndipo inanyamula Kambayo itagwira<br />

chigoba chake n’kuuluka. Ili m’mwambamo,<br />

Nkhwaziyo inakumana ndi Mphamba. Mphambayo<br />

inauza Nkhwaziyo kuti, “Kambatu ndi ndiwo yokoma<br />

kwambiri.” Koma Nkhwaziyo inati, “Ukunena zoona,<br />

komatu chigoba chakechi n’cholimba ngati mwala.”<br />

Ndiyeno Mphambayo inati, “Utangomuponyera<br />

pamwala uwo, chigobacho chikhoza kusweka, ndipo<br />

ife tikhoza kukhwasula vankati.” Nkhwaziyo inamvera<br />

zimenezi ndipo inasiya Kambayo kuti akagwere<br />

pamwalawo moti chigoba chake chinaphwanyika.<br />

Nkhwazi komanso Mphambayo zinasangalala<br />

kwambiri ndi nyama yokoma yomwe zinadya patsikuli,<br />

moti zinachotsa dalazi.<br />

Phunziro: Osapereka moyo wako m’manja mwa mdani.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

109


Mafunso<br />

1. N’chiyani chimene Kamba analakwitsa?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti akanachita chiyani kuti<br />

akafike kunyumba yake yatsopano?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

110


Nkhanu ndi Mwana Wake<br />

Tsiku lina kunacha bwino kwambiri ndipo Nkhanu<br />

inatuluka m’nyumba limodzi ndi mwana wake<br />

n’kupita kukawongola miyendo m’mbali mwa mtsinje.<br />

Koma Nkhanuyo itaona mmene mwana wakeyo<br />

amayendera inati, “Mwana wanga, mayendedwe akowa<br />

sandisangalatsa. N’chifukwa chiyani ukuyenda<br />

cham’mbali? Mpofunika kuti uphunzire kumayenda<br />

mopita kutsogolo. Inetu ndikufuna uziyenda<br />

bwinobwino ngati munthu woti kutsogolo ukukuona.<br />

Sindikufuna uzindichititsa manyazi ndi mayendedwe<br />

ako osalongosokawo.” Koma mwanayo anayankha<br />

kuti, “Chabwino amayi, koma muyambe ndi inuyo<br />

kuchita zimenezi, kuti ineyo ndizitengera chitsanzo<br />

chanu. Anthutu amadabwa akamva munthu akunena<br />

kuti akufuna kusintha dziko, iyeyo akulephera<br />

kudzisintha yekha!”<br />

Phunziro: Osamauza ena kuti achite zomwe iweyo<br />

suchita.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

111


Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti Nkhanu yaikuluyo<br />

inkayenda mopita kutsogolo?<br />

2. N’chifukwa chiyani mwanayo sanagwirizane<br />

ndi zimene kholo lake linanena?<br />

3. Kodi n’zotheka kuthandiza munthu wina<br />

kusintha, ifeyo tikulephera kudzisintha tokha?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

112


Bulu Avala Chikopa cha Mkango<br />

Bulu wina anatola chikopa cha Mkango chomwe alenje<br />

anachiyanika padzuwa kuti chiume. Buluyo anavala<br />

chikopacho ndipo anayamba kuyendayenda m’mudzi<br />

wonse. Anthu komanso nyama zimati zikangomuona,<br />

zinkalikumba liwiro, kufuna kupulumutsa moyo.<br />

Buluyo ataona fumbi limene linabwera chifukwa cha<br />

liwiro la anthu komanso nyama, anasangalala<br />

kwambiri ndipo anayamba kukuwa. Nthawi yomweyo<br />

anthu komanso nyama zinamuzindikira ndipo mwini<br />

Buluyo anabwera n’kuyamba kumukutumula. Kenako<br />

kunabwera Galu n’kuuza Buluyo kuti, “Ayi ndithu,<br />

mtima suvala nsanza. Nthawi zina ngakhale nkhuku<br />

ikhoza kumalota itavala nsapato! Komabe unaitha<br />

bwanawe, chifukwa unapusitsa ambiri. Koma<br />

ukudziwa kuti anakutulukira utangotsegula<br />

pakamwa?”<br />

Phunziro: Zovala zimapusitsa, koma zonena za munthu<br />

m’pamene umadziwa ngati ali wanzeru kapena ayi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

113


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Buluyo anasangalala<br />

pamene anthu komanso nyama zinkathawa?<br />

2. N’chiyani chinachititsa kuti anthu<br />

amuzindikire?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

114


Nkhani ya Mabwenzi a Pamtima<br />

Anthu ena awiri, omwe anali mabwenzi a ponda apo<br />

m’pondepo, anapita kukawongola miyendo<br />

kunkhalango ina, ndipo mwadzidzidzi anakumana ndi<br />

chimbalangondo. Chimbalangondocho chinayamba<br />

kupita kumene kunali anthuwo ndipo anachita<br />

mantha kwambiri. Munthu m’modzi anali kutsogolo<br />

ndipo wina anali m’mbuyo. Munthu anali kutsogoloyo<br />

atangoona kuti chilombocho chikubwera, analumphira<br />

mumtengo n’kubisala ndipo anasiya mnzakeyo ali<br />

pansi pomwepo. Winayo sanalimbanenso n’kuthawa,<br />

koma anangodziponya pansi ndipo nkhope yake<br />

inalowa m’dothi. Chimbalangondocho chinafika pafupi<br />

ndi munthu anagwera pansiyo ndipo chinatsitsa<br />

mphuno yake n’kuyamba kununkhiza mutu wa<br />

munthuyo. Mwamwayi chilombocho sichinamuchite<br />

kalikonse chifukwa chinkaganiza kuti wafa kale, paja<br />

zimbalangondo sizidya kapena kugwira chinthu<br />

chomwe chafa kale. Kenako chinanyamuka<br />

n’kumapita. Chitazimiririka, munthu anali mumtengo<br />

uja anatsika ndipo anafunsa mnzakeyo kuti, “Kodi<br />

bwanawe, chimbalangondo chija chimakunong’oneza<br />

chiyani?” Mnzakeyo anati, “Chinandiuza kuti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

115


ndisamakhulupirire mnzanga amene amandithawa<br />

zikavuta!”<br />

Phunziro: Osamakhulupirira munthu amene<br />

amakukonda zinthu zikakhala zikuyenda bwino, koma<br />

zikavuta amakuthawa.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Chimbalangondocho chinanong’onezadi<br />

munthu anali pansi uja?<br />

2. Kodi munthu anali mumtengo uja akanachita<br />

chiyani akanakhala kuti amamukondadi<br />

mnzakeyo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

116


Mapoto Awiri<br />

Tsiku lina mapoto awiri anasiyidwa m’mbali mwa<br />

mtsinje. Poto m’modzi anali wachitsulo ndipo wina<br />

anali wadothi. Ndiyeno mtsinjewo unadzadza madzi<br />

ndipo mapotowo anayamba kuyandama n’kumapita<br />

ndi madzi. Koma poto wadothiyo ankachita mantha<br />

ndipo ankayesetsa kusambira kuti asagundane ndi<br />

mnzakeyo. Poto wachitsuloyo anayamba kudabwa ndi<br />

zimenezi ndipo anakuwira mnzakeyo n’kumuuza kuti,<br />

“Usaope bwanaweee, sikuti ndikugundayi!” Koma poto<br />

wadothiyo anati, “Ndikuopa kuti ndikhoza kugundana<br />

nawe. Inetu ndinapangidwa ndi dothi, moti utati<br />

undigunde kapena ineyo nditati ndikugunde,<br />

ndingavutikebe ndi ineyo.”<br />

Phunziro: Anthu amphamvu ndi ofooka sangayendere<br />

limodzi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

117


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani tinganene kuti poto wadothi<br />

akanaphwanyika mosavuta akanagundana ndi<br />

mnzakeyo?<br />

2. Perekani zitsanzo za zinthu zamphamvu ndi<br />

zofooka zomwe sizingakhalire pamodzi?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

118


Ng’ombe Zinayi ndi Mkango<br />

Mkango wina unkazembekerera Ng’ombe zinayi zomwe<br />

zinkadya malo ena. Mkangowo unayesa maulendo<br />

angapo kuti ugwire Ng’ombezo koma unalephera.<br />

Unkati ukafuna kuti uukire Ng’ombe imodzi,<br />

Ng’ombezo zinkalozetsana mbuyo ndipo zinkapezeka<br />

kuti Mkangowo wakumana ndi nyanga za Ng’ombezo.<br />

Zikatere Mkangowo unkachita mantha n’kubwerera.<br />

Koma kenako Ng’ombezo zinayambana ndipo iliyonse<br />

inalowera kwake. Zimenezi zinachititsa kuti Mkango<br />

uja upezerepo mwayi, moti unayamba kugwira<br />

Ng’ombe imodziimodzi mpaka zonse zinatha psiti.<br />

Phunziro: Umodzi ndi mphamvu.<br />

Mafunso<br />

1. N’chiyani chinachititsa kuti Mkango usagwire<br />

Ng’ombe pamene zinkachitira zinthu limodzi?<br />

2. Kodi Ng’ombezo zikanatani kuti zisaphedwe ndi<br />

Mkango?<br />

3. Kodi anthu akagawikana, amakhala<br />

amphamvu kapena ayi?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

119


Mneneri Wabodza<br />

Kalekalelo kunali mneneri wina yemwe ankalosera<br />

zam’tsogolo. Ndiye m’nyengo ina ya mvula, mneneriyu<br />

anaona nyenyezi yachilendo ndipo anayamba kuuza<br />

anthu kuti, “Zaka 100 zikubwera kutsogoloku<br />

kudzachitika tsoka loopsa, anthu ambiri adzamwalira<br />

ndipo mudzi wonsewu udzatheratu.” Mneneriyo<br />

ankanena zimenezi akuyang’ana nyenyeziyo ndipo<br />

anaiwaliratu zoyang’ana pamene ankaponda. Ndiye<br />

mwatsoka, pansi panali mwala moti anapunthwa<br />

n’kugwa, nkhope yake n’kulowa m’matope. Anthu<br />

ataona zimenezi anayamba kumuseka ndipo<br />

anamufunsa kuti, “Kodi inuyo mumakwanitsa bwanji<br />

kumalosera zinthu zomwe zidzachitike zaka 100<br />

kutsogoloku, n’kumalephera kudziwa zimene<br />

zangotsala pang’ono kuchitikira phazi lanu? Ndiye<br />

mukufuna tizikhulupirira bodza bodza lofuka utsi<br />

limene mukutiuzali?”<br />

Phunziro: Kumayamba kaye wachotsa chitsotso cha<br />

m’diso lako kenako cha mnzako.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

120


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani anthu aja anayamba<br />

kuseka mneneriyu?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti ankakhulupirira kuti<br />

zimene ananenazo zidzachitikadi? Perekani<br />

chifukwa.<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

121


Msodzi Agwira Nsomba Yaing’ono<br />

Tsiku lina msodzi wina anapita kogwira nsomba koma<br />

sanagwire kathu tsiku lonse. Koma chakumadzulo<br />

anagwira kansomba kakang’ono. Kansombako<br />

kanayamba kupempha msodziyo kuti,<br />

“Ndikhululukireni bwana, ndisiyeni ndizipita. Ineyo<br />

ndidakali mwana, ndachepa kwambiri kuti ndidyedwe.<br />

Mukandibwezeretsa m’madzimu ndikula, ndipo<br />

mukhoza kudzandigwira nditanenepa m’tsogolo. Pa<br />

nthawiyo mukhoza kudzandidya ndili wonona<br />

kwambiri.” Koma msodziyo anati, “Ayi, ayi, sindilola.<br />

Ndagwira iweyo lero. Ndani akudziwa ngati<br />

ndingadzakugwiredi m’tsogolomo?”<br />

Phunziro: Osamawerengera zinthu zomwe sunapeze.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti nsomba yaing’onoyo<br />

ikanalola kuti idzagwidwenso ndi msodziyu ulendo<br />

wina?<br />

2. N’chifukwa chiyani nsombayo inauza msodziyo<br />

kuti amusiye? Kodi inkanena zoona?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

122


Munthu Wadyera Komanso Wansanje<br />

Anthu awiri omwe ankakhala moyandikana nyumba<br />

anapita kwa Mulungu ndipo anapempha Mulunguyo<br />

kuti awapatse zimene akufuna. Mmodzi wa anthuwo<br />

anali wadyera, pomwe winayo anali wansanje. Pofuna<br />

kuwakhaulitsa anthuwa, Mulunguyo anawauza kuti<br />

awapatsa zimene akufuna. Anawauzanso kuti<br />

aziwapatsa zimene akufuna koma anati azipereka<br />

kuwirikiza kawiri zimene m’modzi wapempha. Ndiyeno<br />

munthu wadyera uja anapempha kuti amupatse golide<br />

wodzaza nyumba yake. Pasanapite nthawi anapezadi<br />

golideyo ndipo anasangalala kwambiri. Koma<br />

chisangalalochi sichinakhalitse atazindikira kuti<br />

mnzake wansanje uja wapeza golide wodzadza nyumba<br />

ziwiri. Munthu wansanje uja anamvako bwino<br />

atazindikira kuti mnzake sakusangalala. Koma<br />

ankafuna kuti mnzakeyo akhaule kwambiri, moti<br />

anapempha Mulungu kuti amuchotse mnzakeyo diso<br />

limodzi. Zitatero, Mulungu anamuchotsadi mnzakeyo<br />

diso limodzi, koma zimenezi zinachititsa kuti iyeyo<br />

achotsedwe maso ake onse awiri, moti anakhala<br />

wosaona.<br />

Phunziro: Makhalidwe oipa amabweretsa mavuto.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

123


Mafunso<br />

1. Kodi ndi ndani amene anapezadi zimene<br />

ankafuna?<br />

2. N’chifukwa chiyani anthuwa sankakhutitsidwa<br />

ndi golide amene anali naye?<br />

3. Kodi mungatchule makhalidwe ena oipa amene<br />

amabweretsa mavuto?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

124


Khwangwala Waludzu<br />

Tsiku lina Khwangwala ankafuna kufa ndi ludzu.<br />

Koma mwamwayi anapeza mtsuko wamadzi. Koma<br />

atafika pafupi ndi mtsukowo anapeza kuti madzi ake<br />

anali ochepa ndipo anali pansi penipeni pa mtsukowo<br />

moti sankakwanitsa kuwamwa. Khwangwalayo<br />

anayesetsa kuti amwe madziwo koma analephera moti<br />

kenako anangowasiya n’kutsamira mtsukowo. Koma<br />

kenako nzeru zinamubwerera moti anatola mwala<br />

n’kuponyera mumtsukomo. Anatolanso mwala wina<br />

n’kuponya mumtsukomo ndipo madzi aja anayamba<br />

kukwera. Anapitirizabe kuchita zimenezi mpaka<br />

madziwo anakwera kwambiri ndipo anamwa n’kupha<br />

ludzu lake.<br />

Phunziro: Nyumba imayamba kumangidwa ndi njerwa<br />

imodzi.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi chikanachitika n’chiyani zikanakhala kuti<br />

Khwangwalayo anangokhala osachita chilichonse?<br />

2. Kodi n’chifukwa chiyani nthawi zina sibwino<br />

kutaya mtima mwansanga?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

125


Munthu Wam’nkhalango<br />

M’nyengo ina yozizira kwambiri munthu wina<br />

ankayenda usiku m’nkhalango ndipo anasokonekera<br />

n’kumalephera kupeza njira yakwawo. Ndiye pamene<br />

ankayendayenda m’nkhalangomo anakumana ndi<br />

munthu wina yemwe ankaoneka kuti ankakhala<br />

m’nkhalango momwemo. Munthuyo analonjeza kuti<br />

amupatsa malo ogona usikuwo komanso kuti kukacha<br />

amuthandiza kupeza njira yakwawo. Kenako<br />

munthuyo anamutenga n’kumapita naye kwawo koma<br />

munthu anasokonekera uja anaika manja ake<br />

pakamwa n’kumapemerera ndi mpweya wam’kamwa<br />

mwake. Ndiyeno munthu wam’nkhalango uja<br />

anafunsa kuti, “N’chifukwa chiyani mukupanga<br />

zimenezo?” Munthuyo anayankha kuti, “Manja anga<br />

azizidwa ndiye ndikufuna ndiwatenthetse ndi mpweya<br />

wochoka m’kamwa mwanga.” Kenako anafika<br />

kunyumba kwa munthu wam’nkhalango uja ndipo<br />

pasanapite nthawi anabweretsa phala lotentha<br />

kwambiri kuti mnzake uja adye. Ndiye munthu uja<br />

anayamba kudya phalalo ndipo asanaliike m’kamwa,<br />

ankalipemerera kaye. Ataona zimenezi, munthu<br />

wam’nkhalango uja anafunsa kuti, “Nanga mukuchita<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

126


zimenezo chifukwa chiyani?” Munthuyo anayankha<br />

kuti, “Phalali ndi lotentha kwambiri ndiye ndikuopa<br />

kuti lindiwaula m’kamwa. Choncho<br />

ndikumalipemerera ndi mpweya wam’kamwa mwanga<br />

kuti lizizire.” Atangomva zimenezi, munthu<br />

wam’nkhalango uja anati, “Basi tulukani m’nyumba<br />

mwanga muno! Munthu wamtundu wanji wotuluka<br />

mpweya wotentha komanso wozizira m’kamwa<br />

mwake.”<br />

Phunziro: Mupeze nokha.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mpweya wa munthuyu unali wotentha<br />

kapena wozizira?<br />

2. Kodi kuchita zinthu zimene tinazolowera<br />

n’kulakwa?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

127


Mazira Agolide<br />

Tsiku lina munthu anapita pachisa cha tsekwe ndipo<br />

anapeza dzira looneka lachikasu komanso lowala.<br />

Atalitola anaona kuti dziralo linkalemera kwambiri<br />

moti anaganiza zolitaya poganiza kuti munthu wina<br />

anaikapo mwala kuti amupusitse. Koma kenako<br />

anasintha maganizo ndipo anapita nalo kunyumba<br />

kwake. Atafika kunyumbako anazindikira kuti dziralo<br />

linali lagolide. Kenako anayamba kumapita kuchisa<br />

cha tsekwe chija m’mawa ulionse, ndipo ankatola<br />

dzira limodzi lagolide. Ankati akatola dzira limodzi,<br />

ankaligulitsa moti n’kupita kwa nthawi anakhala<br />

mponda makwacha. Munthuyo atayamba kulemera,<br />

anayamba dyera moti anaganiza zopeza mazira onse a<br />

tsekweyo nthawi imodzi. Choncho, anapha tsekwe uja<br />

n’kumung’amba pamimba ndipo mkati mwake<br />

sanapezemo kanthu.<br />

Phunziro: Dyera limatayitsa zambiri.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

128


Mafunso<br />

1. Kodi munthu wadyerayu ankaganiza kuti<br />

apeza chiyani mkati mwa tsekwe uja?<br />

2. Kodi anapezadi mazira agolide ambiri atapha<br />

tsekweyo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

129


Mbalame Yoimba Mokoma<br />

Kafansiyanji wina ankasowa tulo usiku ndipo<br />

ankangomvetsera mbalame ina ikuimba usiku wonse.<br />

Kaimbidwe ka mbalameyo kanamudolola kwambiri<br />

moti usiku wotsatira anagwira mbalameyo kuti<br />

izimuimbira nthawi zonse. Kenako anaiuza mbalameyo<br />

kuti, “Ndiye popeza ndakugwira, uzindiimbira nyimbo<br />

nthawi iliyonse imene ndikufuna.” Koma mbalameyo<br />

inati, “Mbalame za mtundu wathuwutu sizitha kuimba<br />

nyimbo ngati zikukakamizidwa komanso ngati<br />

zitatsekeredwa m’kanyumba.” Ndiye kenako munthu<br />

uja anati, “Ndiye ndikudyatu! Ndinamva zoti mbalame<br />

ngati iweyo mumakoma kwambiri mukakazingidwa<br />

m’mafuta.” Mbalameyo itangomva zimenezi inati, “Ayi,<br />

musandiphe. Ingondisiyani ndipo ndikuuzani zinthu<br />

zitatu zomwe zingakuthandizeni kwambiri kuposa<br />

kudya kathupi kanga kakang’onoka.” Ndiyeno munthu<br />

uja anaimasula n’kuisiya ndipo mbalameyo inaulukira<br />

panthambi yamtengo wina n’kunena kuti,<br />

“Musadzayerekezenso kumvera lonjezo limene munthu<br />

wogwidwa angadzakuuzeni, chimenechi ndi chinthu<br />

choyamba. Chachiwiri, osamataya kapena kusiya<br />

chinthu chokhacho chimene muli nacho ndipo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

130


chachitatu, osamakhalira kudandaula chinthu<br />

chimene ngakhale mutatani simungachipezenso.”<br />

Mbalameyo itangomaliza kunena zimenezi inauluka.<br />

Phunziro: Osalilira chinthu chimene palibe chomwe<br />

ungachite kuti uchipezenso. Osamada nkhawa ndi<br />

zinthu zimene sungazisithe chifukwa ungangotaya<br />

nthawi yako.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi ndi malangizo ati amene mbalame<br />

inapereka kwa munthu uja?<br />

2. N’chifukwa chiyani munthuyo analakwitsa<br />

kumvera zimene mbalameyo inamuuza?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

131


Nkhandwe, Nkhuku Komanso Galu<br />

Usiku wina Nkhandwe inkazemberera Nkhuku ndipo<br />

Nkhukuyo itazindikira zimenezi, inauluka n’kukwera<br />

mumtengo moti Nkhandweyo inkalephera kuigwira.<br />

Kenako Nkhandweyo inati, “Musaope a Nkhuku,<br />

ndabweratu kuti ndikuuzeni uthenga wabwino.<br />

Mfumu Mkango yalamula kuti pasapezekenso nyama<br />

yodya inzake kuyambira lero. Inati nyama zonse<br />

ziyenera kumakhala limodzi mogwirizana komanso<br />

mwamtendere.” Ndiyeno Nkhukuyo inati, “Uthenga<br />

wake ndi umenewo eti? Chabwino ndamva! Koma pali<br />

wina amene mwina mungakondenso mutamuuza<br />

uthenga umenewu. Mwina nayenso angasangalale<br />

ataumva.” Nkhukuyo inayamba kuyang’ana<br />

kunyumba komwe inkakhala. Ndiyeno Nkhandwe ija<br />

inafunsa kuti, “Kodi kukubwera chiyani?” Nkhukuyo<br />

inayankha kuti, “Kukubwera Galu wa mbuyanga.”<br />

Nkhandweyo itangomva zoti kukubwera galu,<br />

inatembenuka n’kuyamba kuthawa. Ndiyeno<br />

Nkhukuyo inauza nkhandwe ija kuti, “Kodi<br />

mungamuuzenso Galuyo uthenga mwabweretsa uja?”<br />

Koma Nkhandwe ija inati, “Ndikanakonda<br />

ndikanatero, koma ndikuopa kuti Galuyo akhoza<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

132


kundichita zoopsa chifukwa kunalibe pamene Mfumu<br />

Mkango imalengeza zoti pakhale mtendere wa zinyama<br />

zonse.” Nkhukuyo itamva zimenezi inamwetulira<br />

n’kunena kuti, “Nanga ine ndiye ndinaliko?”<br />

Phunziro: Bodza lili ngati matenda, ukhoza kuwabisa<br />

koma pamapeto pake ena amadziwa.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Nkhuku inadziwa bwanji kuti<br />

Nkhandweyo imanama?<br />

2. Kodi Nkhukuyi inaonadi galu wambuyake<br />

akubwera?<br />

3. Kodi ndi makhalidwe oipa ati amene Nkhandwe<br />

inasonyeza m’nkhaniyi?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

133


Munthu Wamanja Lende<br />

Munthu wina ankayendetsa ngolo yake atanyamula<br />

katundu wolemera m’nyengo ina yadzinja. Ngoloyo<br />

inkakokedwa ndi abulu awiri. Chifukwa choti kunali<br />

matope ambiri, matayala a ngoloyo analowa m’matope<br />

n’kutitimira. Ndiyeno munthuyo anayamba kumenya<br />

abulu akewo ndi chikwapu, koma sanakwanitse<br />

kuyenda. Kenako anatopa moti anataya chikwapucho<br />

n’kutsika pangoloyo. Ndiyeno anagwada pansi<br />

n’kupemphera kwa Mulungu kuti amuthandize. Anati,<br />

“Ambuye Mulungu, ndithandizeni chonde pa nthawi<br />

yovutayi.” Koma Mulungu anamuyankha kuti, “Ndiwe<br />

wopusa kwabasi! Tadzuka pamenepo ukakankhe<br />

ngolo yakoyo kuti ichoke m’matopemo!”<br />

Phunziro: Mulungu sangathandize munthu waulesi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

134


Mafunso<br />

1. Kodi tinganene kuti Mulungu anathandiza<br />

munthuyu? Ngati ndi choncho, n’chifukwa chiyani<br />

mwatero?<br />

2. Kodi Mulungu anauza munthuyo kuti achite<br />

chiyani?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

135


Bambo ndi Mwana Wake Apita Kumsika<br />

Bambo wina ankapita ndi mwana wake kukagulitsa<br />

bulu kumsika. Ndiyeno akuyenda kupita kumsikako,<br />

anakumana ndi munthu wina ndipo anawauza kuti,<br />

“Ndinu opusa kwambiri, bwanji osakwera buluyo?”<br />

Ndiyeno bamboyo anakweza mwana wakeyo pabuluyo<br />

n’kumapitiriza ulendo. Koma kenako anakumananso<br />

ndi gulu la anthu ndipo m’modzi mwa anthuwo anati,<br />

“Taonani mwana waulesiyu, iyeyo wakwera bulu koma<br />

bambo ake akuyenda wapansi!” Bamboyo atamva<br />

zimenezi anauza mwana wakeyo kuti atsike ndipo<br />

anakwerapo iyeyo. Koma asanapite patali anakumana<br />

ndi azimayi awiri ndipo m’modzi anawauza kuti,<br />

“Taonani bambo wopanda nzeruyu wakwera bulu,<br />

mwana wake akuyenda wapansi!” Zitatero, bamboyo<br />

anasowa chochita. Koma kenako anaganiza zoti<br />

angokwera pabuluyo limodzi ndi mwana wakeyo.<br />

Pamene ankachita zimenezi n’kuti atayandikira<br />

kumsika kuja ndipo anthu ena anayamba<br />

kuwalozerana n’kumawanena chipongwe. Bamboyo<br />

anatsika pabuluyo n’kuwafunsa kuti alakwa chiyani.<br />

Koma anthuwo anati, “Kodi mulibe manyazi thunthu<br />

lonselo komanso mwana wanuyo kukwera pamsana<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

136


pa bulu wamng’ono ngati ameneyu.” Bambo ndi<br />

mwana wakeyo sanakwerenso buluyo ndipo anaima<br />

kaye n’kuyamba kuganiza zoti achite. Pamapeto pake<br />

anaganiza zodula mtengo n’kumagirira buluyo<br />

n’kumunyamula pamapewa awo. Koma anadabwa<br />

kwambiri kuti anthu ankangowaseka ngati amisala<br />

ndipo posakhalitsa anafika pamlatho wolowera<br />

mumsika ndipo mwendo umodzi wa bulu uja<br />

unamasuka ndipo buluyo anagwa pansi n’kuthawa,<br />

moti sanakwanitsenso kumugwira. Ndiyeno munthu<br />

wina wachikulire, yemwe ankayenda pafupi nawo,<br />

anawauza kuti, “Mutengerepo phunziro, munthu<br />

amene amafuna kusangalatsa onse, sangasangalatse<br />

aliyense.”<br />

Phunziro: Sungakwanitse kusangalatsa aliyense.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani munthu ndi mwana<br />

wakeyu anamanga buluyo pamtengo?<br />

2. Kodi mawu akuti, “Munthu amene amafuna<br />

kusangalatsa onse, sasangalatsa aliyense”<br />

akutanthauza chiyani?<br />

3. Kodi pali nthano iliyonse imene munaimvapo<br />

imene mukuona kuti ikufanana ndi imeneyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

137


4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

138


Munthu Woumira<br />

Kalekalelo panali munthu wina woumira kwambiri<br />

yemwe ankabisa ndalama zake pansi pamtengo<br />

wam’munda mwake. Mlungu ulionse ankapita<br />

pamtengopo n’kukumba ndalamazo, ndipo<br />

ankaziyang’ana kwinaku akunyadira kuti ali ndi<br />

ndalama zambiri. Koma tsiku lina wakuba anamuona<br />

akuchita zimenezi ndipo munthuyu atachoka,<br />

wakubayo anapita kukakumbapo ndalamazo<br />

n’kuthawa nazo. Ndiyeno munthuyu atapitanso kuti<br />

akaone ndalama zake, anapeza kuti zonse zabedwa.<br />

Zitatero anameta tsitsi lake ndipo anang’amba zovala<br />

zake n’kuyamba kulira koopsa. Anthu oyandikana<br />

nawo nyumba atamva kulirako, anabwera kuti<br />

adzaone chimene chachitika. Munthuyo<br />

anawafotokozera zonse zimene zinachitika. Anawauza<br />

kuti anakwirira ndalama zake pansi pamtengowo<br />

ndipo ankabwera mlungu ulionse n’kufukula<br />

ndalamazo moti akaziona mtima wake unkasangalala<br />

zedi. Anthuwo anamufunsa kuti, “Kodi munkatengako<br />

ndalama zina kuti mukagwiritse ntchito?” Munthuyo<br />

anayankha kuti, “Ayi, ndinkangobwera kuti<br />

ndidzazione basi. Ndinkamva bwino kwambiri<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

139


ndikaona ndalama zanga zochuluka.” Ndiyeno<br />

anthuwo anamuuza kuti, “Ndiyetu musasiye. Mlungu<br />

ulionse muzibwerabe pamtengopa ndipo<br />

muzingoyerekezera kuti ndalama zanuzo zidakalipobe.<br />

Zimenezi zikuthandizani kwambiri kuti muzisangalala.<br />

Si mwati munkangobwera kudzaziona?”<br />

Phunziro: Kukhala ndi ndalama kapena zinthu zambiri<br />

koma osamazigwiritsa ntchito, n’chimodzimodzi<br />

osakhala nazo.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani munthu woumirayu<br />

ankakumba ndalama zake nthawi zonse?<br />

2. Kodi akanatani kuti ndalama zake zisabedwe?<br />

3. Kodi akanakhala wanzeru akanachita chiyani<br />

ndi ndalama zakezo?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

140


Nkhandwe ndi Udzudzu<br />

Tsiku lina Nkhandwe inali paulendo ndipo itaoloka<br />

mlatho wina mchira wake unakodwa m’ziyangoyango<br />

moti inkalephera kuchoka. Udzudzu ungapo utaona<br />

zimenezi unakondwera kwambiri ndipo unayamba<br />

kuyamwa magazi a Nkhandweyo popanda<br />

kusokonezedwa ndi mchira wake. Kenako kunabwera<br />

Chisoni ndipo chinamva chisoni kwambiri ndi<br />

Nkhandweyo moti chinapita kuti chikaithandize.<br />

Chinauza Nkhandweyo kuti, “Kodi<br />

ndingakuthandizeko bwanawe pothamangitsa<br />

udzudzu ukukuyamwa magaziwu?” Koma<br />

Nkhandweyo inati, “Zikomo kwambiri pondiganizira<br />

achimwene anga a Chisoni. Koma musatero ayi. Si<br />

mwati mukufuna mungouthamangitsa?” Chisoni<br />

chinavomera ndipo chinafunsa kuti, “N’chifukwa<br />

chiyani simukufuna kuti ndiuthamangitse pomwe<br />

ukukuvutitsani?” Nkhandweyo inayankha kuti,<br />

“Udzudzuwu wangotsala pang’ono kukhuta, ndiye<br />

mukauthamangitsa ukaitana unzake wanjala<br />

kwambiri, moti ubwera n’kudzapopa magazi anga<br />

onse.”<br />

Phunziro: Kumaona patali.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

141


Mafunso<br />

1. N’chiyani chinachititsa kuti Chisoni chimvere<br />

chisoni nkhandwe?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inakana<br />

thandizoli?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

142


Nkhandwe Yopanda Mchira<br />

Tsiku lina mchira wa Nkhandwe unakodwa<br />

pamsampha ndipo pamene inkayesetsa kuti ichoke,<br />

mchirawo unaduka. Poyamba Nkhandweyo inkachita<br />

manyazi kupita pamene panali anzake poopa kuti<br />

azimuseka. Koma kenako inalimba mtima<br />

n’kukakumana ndi anzake onse n’kukawauza kuti<br />

akufuna kuwauza nkhani yofunika kwambiri.<br />

Nkhandweyo inauza anzakewo kuti nawonso adule<br />

michira yawo. Nkhandweyi inafotokoza kuti mchira si<br />

wabwino makamaka agalu akamakuthamangitsa.<br />

Inawafotokozeranso kuti ikunena zimenezo chifukwa<br />

imawaganizira komanso kuwakonda kwambiri.<br />

Inanena kuti sikufuna kuti anzakewo azinyamula<br />

pathupi lawo chinthu chomwe sichingawathandize,<br />

koma kungowabweretsera mavuto. Ndiyeno anzakewo<br />

anati, “Tamva ndithu bwanawe, amenewo ndi<br />

maganizodi abwino. Koma tikuona kuti iweyo<br />

sukanaganiza zotiuza kuti tidule michira yathu,<br />

yomwe ndi ziwalo zamtengo wapatali, zikanakhala kuti<br />

wako sunaduke. Tikuona kuti ukungofuna tifanane!”<br />

Phunziro: Osamakhulupirira malangizo ochokera kwa<br />

munthu amene alibe chimene uli nachocho.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

143


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkafuna kuti<br />

anzake adule michira yawo?<br />

2. Kodi tinganene kuti inkachita zimenezi<br />

powafuniradi zabwino?<br />

3. Kodi tingadziwe bwanji ngati munthu<br />

akutipatsadi malangizo chifukwa choti akutifunira<br />

zabwino?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

144


Kalulu wa Diso Limodzi<br />

Tsiku lina Kalulu anaphulika diso limodzi ndipo<br />

kungochokera pa tsikulo, zinkamuvuta kuona chinthu<br />

chimene chikubwera kuchokera mbali yomwe diso<br />

linaphulikayo. Ndiye pofuna kupewa mavuto,<br />

Kaluluyu ankakonda kudya pafupi ndi phompho lina<br />

lomwe kumunsi kwake kunali nyanja. Ankati<br />

akamadya diso lake labwinobwino lija linkakhala<br />

kumtunda, pomwe mbali inayo inkaloza kunyanja.<br />

Zimenezi zinkathandiza kuti aziona alenje<br />

akamabwera kudzamugwira ndipo nthawi zambiri<br />

ankathawa. Koma mlenje wina anatulukira kuti<br />

Kaluluyo analibe diso limodzi. Ndiye tsiku lina<br />

anakwera bwato n’kulowa m’nyanja, pansi pachitunda<br />

chomwe kalulu ankadyera paja. Kenako anakoka uta<br />

wake n’kubaya Kaluluyo. Kaluluyo analira kuti, “Mayo<br />

ineeeeeee! Zoonadi, imfa sithawika.”<br />

Phunziro: Ngakhale utayesetsa bwanji koma<br />

sungathawe imfa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

145


Mafunso<br />

1. Kodi Kalulu anatani kuti asaphedwe ndi<br />

mlenje?<br />

2. Kodi zimenezi zinathandizadi?<br />

3. N’chiyani chinachititsa Kaluluyu kuganiza kuti<br />

akamadyera malo amenewo akhala wotetezeka?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

146


Msonkhano wa Makoswe<br />

Kalekalelo, Mphaka wina ankavutitsa Makoswe<br />

kwambiri. Makoswewo anayamba kudandaula ndipo<br />

anapanga chimsonkhano cha mnzanga ali pati, kuti<br />

agwirizane zoti achite ndi mdani wawoyo. Atakumana,<br />

Khoswe wina wodziwa kuyankhula anaimirira<br />

n’kunena kuti, “Akuluakulu, Mphakayutu<br />

akutisowetsa mtendere, akutizunza kwabasi moti<br />

tikulephera kupeza chakudya choti tidyetse mabanja<br />

athu. Sindikudziwa kuti tipange bwanji ndi chipsinjo<br />

chatigwerachi?” Nkhaniyo inalowa m’bwalo ndipo<br />

makoswewo anayamba kupereka maganizo<br />

osiyanasiyana. Koma kenako, khoswe wina<br />

wamng’ono anaimirira n’kunena kuti, “Mphakayudi<br />

akutisowetsa mtendere. Mungandivomereze kuti<br />

mdani wathuyu amayenda mochenjera kwambiri moti<br />

umangozindikira wakugwira. Ndiye ngati titamamva<br />

phokoso lotichenjeza kuti akubwera, tikhoza<br />

kumamuzemba, ndipo palibe angagwidwe. Choncho<br />

maganizo anga ndi akuti tipeze belu n’kumumangirira<br />

m’khosi. Ndiyeno akamabwera, ifeyo tizimumva,<br />

tikamumva, tizithawa.” Anzakewo anasangalala<br />

kwambiri ndi mfundo anatsitsayi ndipo anayamba<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

147


kumuwombera m’manja kwinaku akuimba<br />

malikhweru. Kenako Khosweyo anakhala pansi<br />

akumwetulira ndipo ankaoneka kuti wakukhutira ndi<br />

zomwe wanena. Koma Khoswe wina wachikulire<br />

anaimirira n’kunena kuti, “Maganizowa ndi abwinodi.<br />

Koma kodi ndi ndani amene angalimbe mtima kuti<br />

akamuveke belu?” Makoswewo anayamba<br />

kuyang’anizana ndipo palibe anayankha. Kenako<br />

khoswe wachikulireyo anapitiriza kunena kuti, “Ndi<br />

ndani amene moyo sakuufuna? Maganizo ena<br />

amakhala abwino, koma si onse amakhaladi<br />

othandiza.”<br />

Phunziro: Si maganizo onse amene amakhaladi<br />

othandiza.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

148


Mafunso<br />

1. Kodi tinganene kuti maganizo oveka Mphaka<br />

belu, anali abwino kapena ayi? Ngati ndi choncho,<br />

n’chifukwa chiyani?<br />

2. Kodi mwina n’kutheka kuti Makoswe enawo<br />

ananena zotani zomwe zinali zosatheka kuthetsa<br />

vutolo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

149


Mpikisano wa Kalulu ndi Kamba<br />

Nthawi inayake Kalulu ankadzitama kuti ali ndi liwiro<br />

kuposa nyama iliyonse. Ankati, “Palibe anayambapo<br />

wandiposa kuthamanga. Ndikati ndiliyatse liwiro,<br />

ndimachita kukhala ngati mphenzi. Ndipo ndikhoza<br />

kukuuzani kuti panopa palibe amene angandipose<br />

kuthamanga. Ngati pali wina akutsutsa, abwere<br />

tipikisane.” Koma kenako Kamba anayankha kuti,<br />

“Chabwino, tiye tipikisane.” Kaluluyo atamva zimenezi<br />

anati, “Musandiseketse a Kamba! Zoona inuyoooo!<br />

Miyendo yake yolowa mkatiyi? Kayendedwe kanunso<br />

kamakhala ngati ka Mbozi, moti ndikhoza kukusiyani<br />

kuti muuyambe ineyo n’kupha kaye tulo. Kenako<br />

ndikhoza kudzuka, kukasamba, kudya, ndiyeno<br />

n’kuyamba kuthamanga, koma ineyo n’kukakhalabe<br />

woyamba kukafika.” Koma Kamba anati, “Ukhala<br />

chete pambuyo poti ndakuchotsa chimbenene. Tiye<br />

tipikisane!” Choncho anapangana mtunda woti<br />

athamange ndipo aliyense anakonzekera kuyambapo<br />

mpikisanowuo. Lipenga la mpikisanowo litangolira,<br />

Kalulu anatsomphoka ngati mwala walegeni ndipo<br />

posapita nthawi sanaonekenso. Koma<br />

atangothamanga pang’ono, anaima kaye kuti abe tulo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

150


pofuna kumutsimikizira Kamba kuti akucheperakaba.<br />

Kamba uja analimbikira kuthamanga moti pamene<br />

Kalulu ankadzuka, Kambayo anali akudutsa pamzere<br />

womaliza ndipo Kalulu sakanakwanitsa kuthamanga<br />

n’kumupitirira. Ndiyeno Kamba anati, “Munthu<br />

wakhama ndi amene amapambana mpikisano.”<br />

Phunziro: Munthu wakhama akhoza kuchita<br />

chilichonse.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi pakati pa Kalulu ndi Kamba<br />

chimathamanga kwambiri ndi chiyani? Ndiye<br />

n’chiyani chinapambana pampikisanowu, nanga<br />

n’chifukwa chiyani?<br />

2. Kodi pali zinthu zinanso zimene munthu<br />

amene amachita zinthu modekha komanso<br />

mosathamanga angapambane kuposa wachangu<br />

kwambiri?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

151


Gogo Akumana ndi Imfa<br />

Ukalamba umabwera ndi mavuto ambiri ndipo<br />

umapangitsa kuti moyo usamasangalatse. Ndiyeno<br />

kalekalelo, munthu wina anafika potopa ndi ukalamba<br />

chifukwa ankavutika kugwira yekha ntchito<br />

zapakhomo. Ngakhale kuyenda kumene kunkamuvuta<br />

kwambiri. Nthawi zonse ankangokhalira kudandaula<br />

msana, miyendo komanso kuphwanya kwa thupi. Kuti<br />

ayende, ankadalira mgongosera. Ndiye tsiku lina,<br />

anapita kunkhalango kukatola nkhuni zoti aphikire<br />

nandolo. Atamaliza kutola nkhunizo, anazimanga<br />

kamtolo ndipo anasenza n’kumapita kwawo. Koma<br />

kenako nkhunizo zinayamba kumugogoda ndipo<br />

anatopa kwambiri. Atalephera kupirira, anaponya<br />

mtolowo pansi n’kunena kuti, “Sindingakwanitse<br />

kupitirizabe kukhala moyo movutika chonchi!<br />

Ndikanakondwera imfa ikanangobwera<br />

kudzanditenga!” Nthawi yomweyo, imfa inatulukiradi<br />

ndipo inati, “Mayi, ndamva mukutchula dzina langa,<br />

mukundifuna eti? Tsopano ndabweratu, mukufuna<br />

ndikuchitireni chiyani?” Koma gogoyo anati,<br />

“Mwachitadi bwino kubwera. Kodi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

152


mungandithandizeko kusenza mtolowu? Ndikulephera<br />

kuusenza ndekha.”<br />

Phunziro: Zinthu zina zimene timafuna zitachitikadi,<br />

sitingazikonde n’komwe.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi munthu wokalambayu ankafunadi kufa?<br />

N’chifukwa chiyani mukutero?<br />

2. Kodi vuto lake linali chiyani kwenikweni?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

153


Kalulu ndi Anzake Ambirimbiri<br />

Kalulu anali nyama yotchuka kwambiri ndipo anali<br />

ndi anzake ambirimbiri. Koma tsiku lina anaona<br />

Nkhandwe zikubwera ndipo anaganiza zopempha<br />

anzakewo kuti amuthandize kuthawa. Ndiye anapita<br />

kwa Bulu n’kumupempha kuti amunyamule pamsana<br />

pake, koma Buluyo anakana ndipo anamuuza kuti<br />

mbuyake wamuuza kuti agwire ntchito inayake.<br />

Anamuuza kuti, “Ndikuganiza kuti utapempha<br />

Ng’ombe ikhoza kukuthandiza.” Kenako anapita kwa<br />

Ng’ombe akumaganiza kuti iopseza Nkhandwezo ndi<br />

nyanga zake. Koma ng’ombe nayonso inati, “Pepa<br />

m’bale wanga, ndinagwirizana ndi chibwenzi changa<br />

kuti tipite koyenda, ndiye ukudziwa kuti mnyamata<br />

safuna kukhumudwitsa njole yake! Ndikuganiza kuti<br />

utapempha Mbuzi ikhoza kukuthandiza mofanana ndi<br />

mmene ine ndikanachitira.” Koma atapitako, Mbuziyo<br />

inamuyankha kuti ikuvutika msana moti inadandaula<br />

kuti ngati itachita zimene amafunazo ndiye kuti sigona<br />

usiku, ingodziputira zina. Kenako inauza Kaluluyo<br />

kuti Nkhosa ikhoza kumuthandiza pa vuto lakelo<br />

ndipo anapitadi kwa Nkhosa. Koma Nkhosayo<br />

inamuuza kuti, “Ndikanakuthandiza m’bale wanga,<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

154


koma kungoti vuto lakoli landikulira. Ndakhala<br />

ndikumva kuti Nkhandwe zikumadya Akalulu ndi<br />

Nkhosa zomwe. Ndiye ndikuopa kuti nanenso<br />

ndikhoza kusiyana nalo dziko lapansi.” Kenako Kalulu<br />

anapita kwa mnzake womaliza amene ankaganiza kuti<br />

akhoza kumuthandiza. Mnzakeyo anali Tonde. Koma<br />

Tonde nayenso anakana kumuthandiza poganizira<br />

kuti anzake akuluakulu a Kaluluyo anali atakana<br />

kumuthandiza. Tonde ananena kuti kuvomera<br />

ntchitoyo chikanakhala chipongwe kwa nyama zinazo,<br />

zomwe zinali anzake aponda apo m’pondepo a<br />

Kaluluyo. Pa nthawiyi n’kuti Nkhandwe zija<br />

zitayandikira ndipo Kaluluyo anangoti, phazi thandize,<br />

ndipo mwamwayi anapulumukadi.<br />

Phunziro: Munthu amene ali ndi anthu ambirimbiri<br />

ocheza nawo sakhala ndi anzake enieni.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi nyama zomwe Kalulu ankaona kuti anali<br />

anzake apamtima, zinalidi anzake enieni?<br />

2. N’chifukwa chiyani nyamazi sizinkafuna<br />

kuthandiza Kalulu?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

155


Mkango Ugwa M’chikondi<br />

Nthawi ina Mkango unagwa m’chikondi ndi mtsikana<br />

wina wokongola kwambiri ndipo inapita kwa makolo<br />

ake kukafunsira ukwati. Koma anthu a kwawo kwa<br />

mtsikanayo sanadziwe choti anene. Iwo sankafuna<br />

kuti mwana wawo akwatiwe ndi Mkango. Komabe,<br />

ankaopa kuukwiyitsa. Ankadziwa kuti ngati atachita<br />

zinthu mosasamala akhoza kuphedwa. Kenako bambo<br />

a mtsikanayo anati, “Tikuona kuti ndi mwayi waukulu<br />

kuti mwabwera kwathu kuno kudzafunsira banja<br />

monga inuyo Mfumu ya Zinyama zonse. Koma tikuona<br />

kuti mwana wathuyu ndi wamng’ono kwambiri. Ndiye<br />

popeza muzikakhala naye, mukhoza kukamuvulaza<br />

ndi zala komanso mano anuwo. Ndiye timafuna<br />

tikupempheni kuti muwenge zala zanuzo komanso<br />

muzule mano anu akuluakuluwo. Kenako<br />

mudzabwere kudzatenga mtsikanayu kuti akhale<br />

mkazi wanu.” Popeza Mkangowo unakonda kwambiri<br />

mtsikanayo, unachitadi zimene makolowo anapempha.<br />

Unawenga zala zake komanso unachotsa mano ake<br />

akuluakulu. Koma utapita kwa makolo a mkazi uja,<br />

anthu anayamba kuuseka chifukwa cha mmene<br />

unkaonekera komanso chifukwa choti siunkaopsanso.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

156


Phunziro: Chikondi chikhoza kusintha munthu woopsa.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Mkango ukanatani kuti ukwatire<br />

mtsikanayo popanda kuwenga zala komanso<br />

kuchotsa mano ake?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti makolo a mtsikanayo<br />

analola kuti Mkango ukwatire mwana wawo,<br />

Mkangowo utawenga zala komanso kuzula mano<br />

ake? N’chifukwa chiyani mukutero?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

157


Kamtolo ka Mitengo<br />

Bambo wina anadwala kwambiri. Atatsala pang’ono<br />

kumwalira, bamboyo anaitanitsa ana ake kuti awauze<br />

mawu omaliza. Zimadabwitsa kuti anthu ambiri<br />

amadikira kaye kuti atsale pang’ono kutsirizika<br />

n’kumanena mawu omaliza, pomwe anali ndi nthawi<br />

yambirimbiri yoti akanachita zimenezo. Mwina<br />

amachita zimenezi popeza paja amati, mawu<br />

oyankhulidwa ndi munthu yemwe akutsirizika ndi<br />

omwe amatsakamira m’khutu. Ndiye bamboyu anauza<br />

wantchito wake kuti abweretse kamulu ka mitengo<br />

komwe anakamanga pamodzi ndipo anauza ana akewo<br />

kuti, “Tathyolani.” Mwana woyamba anayesetsa kuti<br />

athyole koma analephera. Mwana wachiwirinso<br />

anayesa koma analephera. Ndiyeno bamboyo anauza<br />

anawo kuti, “Tsopano masulani mitengoyo. Ndipo<br />

aliyense atenge kamtengo kamodzi.” Anawo atachita<br />

zimenezi, anawauza kuti, “Thyolani.” Anawo anathyola<br />

timitengoto mosavuta ndipo bamboyo anati, “Mwaona<br />

zimene zachitika? Mtengo suvuta kuthyola ukakhala<br />

wokha, koma ikakhala yambiri, imakhala yolimba<br />

kwambiri moti munthu sungaithyole. Nanunso<br />

muphunzirepo kanthu. Dziwani kuti ngati mutayamba<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

158


kukangana aliyense n’kuyamba kuchita zake, zinthu<br />

sizidzakuyenderani bwino. Nanunso mukapanda<br />

kusamala anthu adzakuthyolani ndipo mafupa anu<br />

adzalira gobedee!”<br />

Phunziro: Mu umodzi muli mphamvu.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi n’chifukwa chiyani zinali zophweka ana<br />

aja kuthyola mtengo umodziumodzi?<br />

2. Kodi tinganene kuti ana a bamboyu anali ngati<br />

mitengo imeneyi chifukwa chiyani?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

159


Mawu Omaliza a Mkango<br />

Nthawi ina Mkango unadwala mwakayakaya ndipo<br />

utatsala pang’ono kufa, unaitana nyama zonse kuti<br />

uziuze mawu omaliza. Unanena kuti izilowa nyama<br />

imodziimodzi kuphanga lake. Choncho Mbuzi inapita<br />

kuphanga la Mkango ndipo inamvetsera kwa nthawi<br />

yaitali mawu omaliza a Mkangowo. Kenako Nkhosa<br />

inakalowa ndipo kenako Ng’ombe nayonso inalowa<br />

kuti ikamve mawu omaliza a Mfumu ya Zilombo zonse.<br />

Phangalo silinkadziwika kuti ndi lalikulu bwanji<br />

chifukwa munali m’dima wa tsokomola<br />

ndingakuponde. Komabe nyamazo zinapitiriza kulowa<br />

m’phangalo. Koma kenako, Mkango uja unayamba<br />

kuchira moti unadzuka n’kuima pakhomo la phanga<br />

lake ndipo unaona Nkhandwe ikudikira panja pa<br />

phangalo. Ndiyeno unafunsa Nkhandweyo kuti,<br />

“N’chifukwa chiyani sukubwera kudzamva mawu anga<br />

omaliza?” Koma poyankha Nkhandweyo inati, “Pepani<br />

mfumu yanga, pansipa pakuoneka mapazi a nyama<br />

monga Mbuzi, Nkhosa komanso Ng’ombe, ndipo<br />

zikuoneka kuti nyamazi zalowa m’phanga lanulo.<br />

Koma sindikuona mapazi a nyamazi zikutuluka.<br />

Zimenezi zinandisokoneza mutu kwambiri, moti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

160


ndinayamba kuchita mantha. Mantha amenewa<br />

akhoza kutha ngati mutatulutsa nyama zonse zomwe<br />

zalowa m’phanga lanulo. Ngati mutatero ndiye<br />

mukhoza kundimasura moti nanenso ndikhoza<br />

kubwera kuti ndidzamve mawu anu omaliza.”<br />

Phunziro: N’zosavuta kugwera m’manja mwa adani<br />

koma zimakhala zovuta kutulukamo.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi chinachitika n’chiyani ndi nyama zomwe<br />

zinalowa m’phanga la Mkango lija?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti Mkango unkadwaladi?<br />

N’chifukwa chiyani mukutero?<br />

3. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkakayikira zoti<br />

Mkango umadwaladi mwakayakaya?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

161


Ubongo wa Mbawala<br />

Tsiku lina Mkango unagwirizana ndi Nkhandwe kuti<br />

zipite kosaka. Mkangowo unali utatumiza uthenga<br />

kwa Mbawala woiuza kuti nkhandwe ikufuna<br />

kukhazikitsa mtendere ndi Mbawalayo. Ndiyeno<br />

Mbawala itafika pamalo omwe anagwirizana kuti<br />

akakumane, inasangalala kwambiri kuona kuti<br />

Mkango nawonso wabwera monga mkhalapakati wa<br />

mgwirizanowu ndipo inaona kuti yalemekezedwa<br />

kwambiri ndi Mfumu ya Nyama zonse. Mbawalayo<br />

inati, “Ndafika kalekaletu pano, paja a mvula zakale<br />

anati kambalame kolawira ndi kamene kamatola<br />

mphutsi!” Nkhandwe itamva zimenezi inamwetulira<br />

n’kunena kuti, “Komatu khoswe wachiwiri ndi amene<br />

amadya zomwe zili pamsampha! Woyamba amafa<br />

atavuvutidwa ndi msamphawo.” Ali mkati<br />

mokambirana zimenezi, Mkango uja unagwira<br />

Mbawalayo n’kuipha ndipo unauza Nkhandwe ija kuti,<br />

“Chakudya chathu chalero ndi chimenechi. Ndikufuna<br />

kuti uziyang’anira nyamayi, ineyo ndikabe kaye tulo<br />

pang’ono. Ndiye popeza ukudziwa zimene ndimachita<br />

ndi anthu osamvera, usayerekeze n’komwe kukhudza<br />

nyamayi.” Mkangowo unachokadi ndipo Nkhandweyo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

162


inkayang’anira nyamayo. Koma patapita nthawi,<br />

Nkhandweyo inayamba kumva njala. Ndiye itaona kuti<br />

Mkango sukubwera, inaganiza zochotsa ubongo wa<br />

Mbawalayo n’kuudya. Posapita nthawi, Mkango uja<br />

unatulukira ndipo utayang’ana bwinobwino,<br />

unazindikira kuti ubongo wa Mbawalayo<br />

wachotsedwa. Kenako unafunsa Nkhandweyo<br />

mwaukali kuti, “Kodi iwee, ubongo wa nyamayi<br />

wausiya kuti?” Koma Nkhandweyo inayankha kuti,<br />

“Mbawalayitu inalibe ubongo, chifukwa ikanakhala<br />

kuti inali ndi ubongo, sikanabwera pano. Ikanayamba<br />

yaganiza kaye kuti chilengere Mulungu dziko,<br />

zinachitikapo liti Mbawala kupanga mgwirizano ndi<br />

Nkhandwe, mkhalapakati wakenso n’kukhala<br />

Mkango.”<br />

Phunziro: Munthu wanzeru sasowa choyankha.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi nzeru za Nkhandwe zinamuthandiza<br />

bwanji kudziwa zoyankha?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti Mkangowo<br />

unangoisiyasiya Nkhandweyo?<br />

3. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

163


<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

164


Nkhwazi Ibayidwa ndi Muvi<br />

Tsiku lina Nkhwazi inkauluka ndipo mwadzidzidzi<br />

inangozindikira kuti yabaidwa ndi muvi moti inavulala<br />

kwambiri. Kenako inayamba kugwa pansi ndipo<br />

magazi ankangoti chuuu kuchucha kuchokera<br />

pamene inabaidwapo. Itayang’ana pamene<br />

inabaidwapo inaona kuti muviwo unali<br />

utamangiriridwa ndi nthenga yake. Ndiye pamene<br />

inkafa inanena kuti, “Nthawi zambiri timapereka kwa<br />

adani athu chida choti atiphere.”<br />

Phunziro: Nthawi zina timapereka kwa adani anthu<br />

chida choti atiphere.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi ndi chiyani chimene mwina n’kutheka<br />

Nkhwazi inapereka kwa mdani wake chimene<br />

chinaiphetsa?<br />

2. Kodi mdani wa Nkhwaziyi ndi ndani?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

165


Kuwerengera Madzi a Mphutsi<br />

Tsiku lina mtsikana wina ananyamula mtsuko<br />

wodzadza ndi mkaka pamutu pake kuti akagulitse<br />

kumsika. Koma ali m’njira, anayamba kuganizira<br />

zomwe angachite ndi ndalama zomwe angapeze<br />

akagulitsa mkaka womwe anasenzawo. Anati,<br />

“Ndikakangougulitsa, ndikagula nkhuku kwa Angozo.<br />

Nkhukuzo zikakula, zidzayamba kuikira mazira<br />

ambirimbiri ndipo akadzachuluka, ndidzawagulitsa<br />

kwa a Nankhoma. Ndalama zomwe nditadzapeze<br />

ndikadzagulitsa mazirawo ndidzagula diresi yokongola<br />

komanso mpango woti ndizidzavala kumutu.<br />

Ndikuganiza kuti ndikamadzayenda nditavala<br />

zimenezi, anyamata onse azidzangondilondola.<br />

Sindikukayikira kuti Nachisale akadzaona zimenezi<br />

adzachita nsanje. Koma aa, ndizidzangokhala ngati<br />

sizikunditani, sindikundikhudzaaa!<br />

Ndizidzangomuyang’ana cham’mbali kwinaku<br />

ndikuyendetsa mutu wangawu chonchi . . . ” Nthawi<br />

yomweyo mtsuko unali pamutu uja unagwa pansi<br />

n’kusweka, ndipo mkaka wonse unataika. Zitatere<br />

anabwerera kwawo akulira n’kukawauza mayi ake<br />

zomwe zinachitika. Atamva zimene mwana wawoyo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

166


ananena, mayiwo anati, “Mwana wanga,<br />

osamawerengera zinthu zimene sunazipeze.”<br />

Phunziro: Osamawerengera madzi a mphutsi.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani mtsikanayu ankaganiza<br />

kuti mkaka wodzadza mtsukowo umuthandiza<br />

kuti adzagule diresi komanso mpango?<br />

2. Kodi akanatani kuti asagwetse mtsukowo?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

167


Hatchi ndi Bulu<br />

Tsiku lina Hatchi ndi Bulu zinkayendera limodzi.<br />

Hatchi inkayenda mwamatama pomwe Bulu anali<br />

atanyamula katundu wambirimbiri moti anali<br />

atalemedwa zedi. Bulu anadandaula kuti,<br />

“Ndimalakalaka ndikanakhala ngati iwe. Sugwira<br />

ntchito iliyonse, koma umapatsidwa zakudya zambiri<br />

komanso zonse zimaoneka kuti zimakuyendera<br />

bwino.” Ndiyeno tsiku lotsatira kunayambika<br />

nkhondo, ndipo Hatchiyo inatengedwa n’kupita<br />

kunkhondo moti ili kumeneko inavulala kwambiri<br />

n’kutsala pang’ono kufa. Bulu uja atamva zimene<br />

zinachitikazo anati, “Inetu ndimadzinamiza. Kuli<br />

bwino kumakhala movutika uli pamtendere kusiyana<br />

n’kumadya bwino moyo wako uli pachiswe.”<br />

Phunziro: Moyo ndi wofunika kwambiri kuposa<br />

chilichonse.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Bulu ankachitira nsanje<br />

Hatchi?<br />

2. Bulu ananena kuti Hatchi sinkachita<br />

chilichonse. Kodi ankanena zoona? Ngati<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

168


sankanena zoona, kodi Hatchi inkagwira ntchito<br />

yanji?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

169


Woliza Lipenga<br />

Tsiku lina munthu woliza lipenga kunkhondo<br />

anayandikira kwambiri adani ndipo anamugwira.<br />

Atangotsala pang’ono kumupha, munthuyo<br />

anapempha anthuwo kuti amuchitire chifundo. Anati,<br />

“Inetu sindimenya nawo nkhondo, ndipo sindinyamula<br />

chida chilichonse. Ndimangonyamula chitolilochi.<br />

Nanga chimenechi ndingaphere munthu ngati? Ndiye<br />

ndichitireni chifundo, musandiphe, chifukwa nanenso<br />

sindipha anthu!” Koma anthuwo anati, “N’zoona kuti<br />

sumenya nawo nkhondo, koma umalimbikitsa<br />

komanso kutsogolera asilikali kuti amenye nkhondo,<br />

ndiye tikupha pa chifukwa chimenechi.”<br />

Phunziro: Tikhoza osachita nawo zoipa, ngati zonena<br />

zathu zimalimbikitsa ena kuchita zimenezo,<br />

n’chimodzimodzi kuti nafenso timachita zinthuzo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

170


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani woliza lipenga ankaganiza<br />

kuti adani akewo samupha?<br />

2. Koma kodi woliza lipengayo akanapangitsa<br />

bwanji kuti adani akewo akumane ndi mavuto?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

171


Katswiri Wolira Nyama Zosiyanasiyana<br />

Pachikondwerero china, katswiri wina woyerekeza<br />

kulira kwa zinyama anaseketsa anthu kwambiri<br />

pamene ankalira nyama zosiyanasiyana. Pomaliza<br />

munthuyo analira ngati nkhumba ndipo anthu<br />

anasangalala kwambiri moti ankaganiza kuti ikulira<br />

ndi nkhumba yeniyeni. Ndiyeno munthuyo anaima<br />

kaye n’kunena kuti, “Kumeneku ndi kulira kwa<br />

nkhumba. Ngati mukukayikira kuti ndimaliradi ndi<br />

ineyo, mawa mudzakhale pomwepo kuti mudzamve<br />

kulira kwa nkhumba yeniyeni.” Anthuwo atamva<br />

zimenezi anaseka kwambiri ndipo tsiku lotsatira<br />

munthu uja anabweranso. Koma pa nthawiyi anabisa<br />

mwana wankhumba ndipo anawerama<br />

n’kumamukoka khutu. Mwana wankhumbayo<br />

anayamba kulira ndipo anthuwo atamva kulirako<br />

anayamba kumugenda n’kumauza munthuyo kuti<br />

asiye. Munthuyo anati, “Ndinu wopusa kwabasi.<br />

N’chifukwa chiyani mumasangalala munthu<br />

akamayerekeza kulira kwa nyama n’kumadana ndi<br />

kulira kwa nyama yeniyeniyo?”<br />

Phunziro: Anthu amasangalala ndi kuyerekezera<br />

chinthu chinachake n’kumadana ndi chinthucho.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

172


Mafunso<br />

1. Kodi katswiriyu ankapanga chiyani chomwe<br />

chinkaseketsa anthu?<br />

2. N’chifukwa chiyani anthu aja anakwiya ataona<br />

kuti imene imalirayo inali nkhumba yeniyeni?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

173


Nkhandwe ndi Mbuzi<br />

Tsiku lina Nkhandwe inkayendayenda m’nkhalango<br />

ndipo mwatsoka inagwera m’mbuna ndipo inkalephera<br />

kutulukamo. Ndiyeno zinachitika kuti Mbuzi<br />

inkadutsa pafupi ndi mbunayo ndipo Mbuziyo itaona<br />

Nkhandweyo inafunsa kuti, “Kodi mukutani<br />

m’menemo?” Nkhandweyo inayankha kuti, “Chaka<br />

chino kukhala chilala choopsa moti madzi azisowa.<br />

Ndiye ndikukumba chitsimechi kuti chilalacho<br />

chikamafika, ndikhale ndili ndi madzi okwanira.<br />

Nawenso dumphira momwemuno tithandizane kuti<br />

tizidzamwera limodzi madziwa.” Mbuziyo itamva<br />

zimenezi inaona kuti umenewo ndi mwayi wake, moti<br />

inalumphiradi m’mbunamo. Kenako Nkhandwe ija<br />

inalumphira pamsana pambuziyo n’kutuluka<br />

m’dzenjemo ndipo inati, “Tionana bwanawe.<br />

Kuyambira lero usadzayerekezenso kumvera<br />

malangizo ochokera kwa munthu yemwe wapanikizika<br />

ndi mavuto.”<br />

Phunziro: Osamakhulupirira malangizo ochokera kwa<br />

munthu amene wapandikizika, akhoza kukhala kuti<br />

akungofuna njira yothawira mavutowo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

174


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Mbuzi inadumphira<br />

m’dzenje muja?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nkhandwe inkafuna kuti<br />

Mbuziyo igwere m’dzenjemo?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

175


Nsikidzi ndi Ana Ake<br />

Munthu wina atatopa kulumidwa ndi Nsikidzi,<br />

anaganiza zotereka madzi kuti azikhaulitse. Kenako<br />

anatenga bulangete lakelo n’kuliika munkhali<br />

n’kutenga madzi obwadamuka n’kuwakhuthulira<br />

momwe munali bulangetelo kuti nsikidzizo zikhaule.<br />

Ndiye zimenezi zitangochitika, Nsikidzi yomwe inali<br />

m’bulangetemo inauza ana ake kuti, “Ana anga,<br />

muyenera kukhala opirira, chifukwa chilichonse<br />

chotentha, pamapeto pake chimazizira. Vuto<br />

lingatenthe bwanji, limakhala ndi mapeto ake.”<br />

Phunziro: Chilichonse chotentha, pamapeto pake<br />

chimazizira. Mavuto angakule bwanji, amakhala ndi<br />

polekezera.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi munthu anatani Nsikidzi zitamuvuta zedi?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nsikidzi inauza ana ake<br />

kuti “chilichonse chotentha, pamapeto pake<br />

chimazizira”?<br />

3. Kodi ndi zoona kuti vuto lililonse limakhala ndi<br />

pothera?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

176


Nyani ndi Mwana Wake<br />

Nthawi inayake, padziko lapansi panachitika<br />

mpikisano woonetsa ana okongola kwambiri. Ndiye<br />

Nyani atangomva za mpikisanowu, nayenso anatenga<br />

mwana wake n’kuthamangira komweko. Malamulo a<br />

mpikisanowo anali akuti, usanayambe kuchita nawo<br />

mpikisanowo unkafunika kukaonetsa mwana wako<br />

kwa wochititsa mpikisanowo. Ndiye wochititsa<br />

mpikisanowo ataona mwana wa Nyaniyo anaseka<br />

koopsa, ndipo anafunsa Nyaniyo kuti, “Mayi,<br />

mwabweretsachi n’chiyani?” Nyaniyo anayankha kuti,<br />

“Mwana, bwanji?” Wochititsa mpikisanowo anati,<br />

“Nanga bwanji mphunozi?” Akuti ankaseka mphunozo<br />

chifukwa zinkangooneka ngati zochita kuboola ndi<br />

tchizulo. Kenako anapitirizabe kuseka mwachipongwe<br />

kwambiri. Koma kenako Nyaniyo anati, “Inuyo<br />

mukhoza kuseka mmene mungathere. Koma dziwani<br />

kuti kwa ineyo, padziko lonse lapansili palibenso<br />

mwana wina wokongola kwambiri kuposa wangayu!”<br />

Phunziro: Mwana sanyansa mayi wake. Anthu ena<br />

akhoza kumamuona kuti ndi wonyansa, koma kwa<br />

mayi wake ndi wokongola kwambiri.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

177


Mafunso<br />

1. Kodi tinganene kuti Nyani ankaonadi kuti<br />

akhoza kupambana mpikisanowo?<br />

2. N’chifukwa chiyani wochititsa mpikisanowu<br />

anaseka ataona mwana wa Nyaniyo?<br />

3. Kodi nyaniyo anayankha zotani?<br />

4. Kodi wochititsa mpikisanowu analakwitsa<br />

chiyani?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

178


Nkhuku ndi Mwala Wamtengo Wapatali<br />

Tsiku lina Tambala ankayendayenda kwinaku<br />

akusaka chakudya. Kenako anafukula kanthu<br />

kenakake kowala pakati pazinyalala. Ndiyeno anati,<br />

“Ho! ho! Mulungu sapatsa pamanja!” Kenako<br />

anakachotsa pazinyalalapo ndipo anazindikira kuti ndi<br />

kamwala kamtengo wapatali. Ndiyeno anati, “Ukhoza<br />

kukhaladi wamtengo wapatali kwa anthu amene<br />

amakuona ngati mwala wapadera. Koma kwa ineyo,<br />

chinthu chamtengo wapatali ndi deya kapena misere<br />

imene imandithandiza kuti ndikhale ndi moyo!”<br />

Phunziro: Chinthu chimakhala chamtengo wapatali<br />

malinga ndi mmene munthu akuchionera.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mukuganiza kuti tambala ankaganiza kuti<br />

wapeza chiyani?<br />

2. Kodi chinthu chamtengo wapatali chimene<br />

tambalayu ankafunafuna chinali chiyani?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

179


Khoswe ndi Msampha<br />

Bambo wina makoswe anamuvuta zedi ndipo amati<br />

akagula chinthu, Makoswewo ankamubera<br />

n’kukalowetsa kuuna wawo. Tsiku lina makoswewo<br />

anamusautsa kwambiri chifukwa<br />

ankaongoyendayenda padenga moti tulo sadatione.<br />

Zinafika pomukwana kwambiri Makoswewo<br />

atamuboolera zovala zake ndipo anaganiza zothana<br />

nawo. Anayesa kuwathirira tameki, koma palibe ndi<br />

m’modzi yemwe amene anadya. Kenako anaganiza<br />

zotchera misampha. Anaika misampha ingapo<br />

m’nyumbamo ndipo pamsampha uliwonse anaika<br />

chakudya chomwe Makoswewo ankachikonda<br />

kwambiri. Makoswewo ataona zimenezi, anakopeka<br />

kwambiri moti khoswe wina anati, “Tiyeni<br />

tikasangalale ndi chakudya!” Koma mnzake anamuuza<br />

kuti, “Taima kaye bwanawe, wadziwa bwanji kuti<br />

tikasangalala. Kodi munthuyu anayamba wachitazo<br />

zimenezi? Mwinatu akufuna atikole.” Koma Khoswe<br />

wina wadyera kwambiri sanaupeze mtima, moti<br />

anaganiza zotenga chakudya chomwe chinali<br />

pamsampha wina. Atangochigwira, msamphawo<br />

unafwamphuka ndipo unamukang’antha pamimba.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

180


Khosweyo anayamba kulira ndipo anauza anzakewo<br />

kuti, “Chakudyachi ndilibe nachonso ntchito,<br />

mukhoza kuchitenga. Chomwe ndikufuna panopa ndi<br />

kuchoka pamsamphawu.”<br />

Phunziro: Kumaganizira zotsatira za zomwe<br />

mukuchita. Osamangotengeka ndi chilichonse.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi khoswe wadyera anatengeka ndi chiyani?<br />

2. Kodi ananena chiyani atapanidwa ndi<br />

msampha?<br />

3. Kodi tinganene kuti sankachifunadi<br />

chakudyacho? N’chifukwa chiyani anasintha<br />

maganizo?<br />

4. N’chifukwa chiyani tiyenera kumaganizira<br />

mavuto amene tingakumane nawo tisanachite<br />

chilichonse?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

181


Nkhani ya Kutha kwa Dziko<br />

Kagiso anali ndi mbuzi ndipo pa nthawiyi n’kuti<br />

itakula ndithu. Ndiye tsiku lina kunabwera anzake<br />

omwe ankakhala moyandikana nawo nyumba<br />

n’kumuuza kuti aphe mbuziyo. Atawafunsa chifukwa<br />

chake, anthuwo anamuuza kuti, “Nkhosa yakoyitu<br />

yanenepa. Tiye tikaiphe kumtsinje. Popeza kunjaku<br />

kwatentha, tikaiphere kumtsinjeko kuti<br />

tikakatenthedwa tizikangolowa mumtsinje<br />

n’kumasambira.” Koma Kagiso anawayankha kuti,<br />

“Ayi, sindikufuna kupha mbuzi yanga.” Koma wina<br />

anamuuza kuti, “Kodi sunamve? Dzikolitu likutha<br />

mawa!” Kagiso anadabwa ndi zimenezi ndipo ataona<br />

kuti akhoza kufa asanadye mbuzi yake, anavomera<br />

zoipha ndipo anaigwira n’kumapita nayo kumtsinje.<br />

Atafika kumeneko anaipha ndipo anayamba kuisenda<br />

chikopa. Anzake aja atayamba kumva kutentha<br />

anavula zovala zawo zonse n’kuyamba kusambira.<br />

Koma Kagiso ankangoti jijirijijiri kukonza mbuzi ija.<br />

Atamaliza kuikonza, anakoleza moto ndipo anayamba<br />

kuiwotcha. Pa nthawiyi n’kuti anzake aja akupanga<br />

chipako cham’madzi. Patapita nthawi, kafungo<br />

kabwino kanayamba kumveka ndipo anzake aja<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

182


anatuluka m’madzi muja n’kumuuza kuti, “Koma<br />

ndiye utipha ndi fungotu, tigawireko titsuke<br />

m’kamwa.” Koma atayang’ana pamene panali zovala<br />

zawo anaona kuti palibe ndipo anamufunsa kuti,<br />

“Kodi zovala zathu wazisiya kuti?” Kagiso anayamba<br />

kuzimbaitsa nkhaniyi amvekere, “Inetu ndimadabwa<br />

anthu akamanena kuti zovala. Ndimaona kuti munthu<br />

akavula zimene anavala n’kuziika poteropo,<br />

sizikhalanso zovala, koma zovula.” Anzakewo atamva<br />

zimenezi anakwiya kwambiri ndipo anamuuza kuti,<br />

“Usatitayitse nthawi iweeee! Zovala zathu wazisiya<br />

kuti?” Ndiyeno Kagiso anayankha kuti, “Ndazikolezera<br />

moto!” Atamva zimenezo anzakewo anapsa mtima<br />

kwambiri ndipo anati, “Zoona ungakolezere moto<br />

zovala zathu?” Koma Kagiso anayankha kuti, “Ee, pali<br />

vutoo? Si paja munati dziko likutha mawa, ndiye<br />

mukufunanso zovala zantchito yanji?” Anzakewo<br />

anangoti kukamwa yasaa, ndipo anayamba kuganizira<br />

mmene angayendere kuti akafike kwawo.<br />

Phunziro: Nthawi zina ukamapusitsa mnzako,<br />

umakhalanso ukudzipusitsa wekha.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

183


Mafunso<br />

1. Kodi zimene anzake a Kagiso ankanena, zoti<br />

dziko likutha mawa, zinali zoona? N’chifukwa<br />

chayani mukutero?<br />

2. N’chifukwa chiyani Kagiso anakolezera moto<br />

zovala za anzakewo?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

184


Nkhani ya Kalulu ndi Nkhandwe Yatulo<br />

Iyi ndi nkhani ya achikulire a Kalulu ndi Nkhandwe.<br />

Tsiku lina Kalulu ankafuna kupusitsa Nkhandwe<br />

ndipo anaima pafupi ndi mwala wina. Mwalawo<br />

unaima ngati ukufuna kugwa ndipo Kalulu<br />

ankaukankhira m’mwamba. Nkhandwe itaona<br />

zimenezi inafunsa Kalulu kuti, “Achikulire, mukutani<br />

pamenepo?” Ndiyeno Kalulu anaiuza kuti, “Tabwera<br />

mwamsanga bwanawe, mwalawutu ukugwa. Taugwira<br />

kuti ineyo ndikatenge mtengo tidzauimikire.”<br />

Nkhandweyo inavomeradi ndipo Kaluluyo<br />

ananyamuka n’kumapita n’kuisiya Nkhandwe itagwira<br />

mwalawo. Nkhandweyo inachita zimenezi kwa nthawi<br />

yaitali zedi koma Kalulu uja sanabwererenso.<br />

Nkhandweyo inayamba kuitana Kalulu uja ndipo<br />

inkati, “Kodi simunaupezebe mtengowo, mwalawutu<br />

ukundilemera.” Koma kunali zii. Nkhandweyo<br />

itatheratu, inaganiza zosiya mwalawo. Inausiya<br />

mwachanguchangu n’kuchokapo kuti usaigwere.<br />

Koma itachoka, inaona kuti mwalawo sunasunthe.<br />

Ngakhale inaona zimenezi, Nkhandweyo sinatengerepo<br />

phunziro. Tsiku linanso Kalulu anapita kukamwa<br />

madzi padziwe lina ndipo m’madzi munkaoneka<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

185


mwezi. Apa anaganizanso zopusitsa Nkhandwe ija<br />

ndipo anaiitana n’kuiuza kuti, “Taona m’madzimo,<br />

pansi pamadzipo, chimenechotu ndi chakudya.”<br />

Ndiyeno Nkhandweyo inati, “Ee, ndachiona, ndi<br />

chakudya chanji?” Kaluluyo anayankha kuti, “Ndi<br />

mtanda wa nsima. Kuteroko ineyo ndayamba kale<br />

kumwa madziwa n’cholinga choti aphwe. Ndiye popeza<br />

ndiwe wamkulu, ukhoza kumaliza madzi atsalawa,<br />

kuti kenako titenge nsimayo tidye. M’bale wanga,<br />

tamwa madziwa kuti timeze kadaunda madzi.”<br />

Nkhandwe yatuloyo inavomeranso zimenezi ndipo<br />

inayamba kumwa madzi aja. Sinazindikire kuti<br />

chimene chimaoneka m’madzicho si nsima koma<br />

mwezi. Kenako kalulu uja anatsanzika n’kumapita.<br />

Nkhandweyo inamwa madziwo mpaka mimba yake<br />

inangoti nguu, kukhuta. Itaona kuti sakuthapo,<br />

inangonyamuka n’kumapita kwawo ndipo usiku wa<br />

tsiku limenelo sinatione tulo chifukwa cha kupweteka<br />

kwa mimba yake.<br />

Phunziro: Osalola kuti munthu akupusitse kawiri.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

186


Mafunso<br />

1. Kodi Kalulu anapusitsa bwanji Nkhadwe?<br />

2. N’chiyani chikusonyeza kuti Nkhandweyo inali<br />

yatulo?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

187


Anyamata Awiri Akumana ndi Wokalamba<br />

Kalekalelo panali anyamata awiri a pachibale.<br />

Anyamatawa anaganiza zoyamba kuyendayenda<br />

padzikoli kuti akafunefune mwayi komanso<br />

chisangalalo. Ali m’njira anaona bambo wina<br />

wachikulire akuyenda patsogolo pawo. Bamboyu anali<br />

ndi ndevu zowirira zedi. Ndiyeno mnyamata wamkulu<br />

anati, “Wamuona bambo uyo? Alitu ndi ndevu zoti<br />

ndikhoza kuzendewera. Ndevu zopangitsa mwana<br />

kufunsa kuti, ‘Ababa pakamwa mpati?’ Mwina<br />

mwachidule ndingoti ali ndi ndevu za ponya mtedza<br />

upaone.” Anyamatawo ankachita chidwi ndi ndevuzo<br />

moti bamboyo anaima n’kuwafunsa kuti, “Mukupita<br />

kuti?” Anyamatawo anamufotokozera chimene<br />

ankafuna ndipo bamboyo anati, “Ndikhozatu<br />

kukuthandizani.” Kenako anapisa m’thumba<br />

n’kutulutsa kajumbo kodzadza ndi ndalama. Kenako<br />

anafunsa anyamatawo kuti, “Ndani amene akufuna<br />

ndalamazi?” Nthawi yomweyo mnyamata wamkulu uja<br />

anayankha kuti, “Ndipatseni ine!” Bamboyo<br />

anamupatsadi ndipo kenako anapisanso m’thumba<br />

n’kutulutsa mwala wamtengo wapatali ndipo<br />

anafunsaso kuti, “Ndani akufuna mwala wamtengo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

188


wapataliwu?” Nthawi yomweyo mnyamata wamkulu<br />

uja anayankhanso kuti, “Ndipatseni ine!” Bamboyo<br />

anamupatsadi. Koma mnyamata wamng’ono uja<br />

sanalandire kanthu. Ndiyeno bambo wachikulireyo<br />

anatula thumba limene ananyamula n’kupempha<br />

anyamata awiriwo kuti, “Ndani amene<br />

atandinyamulire thumbali kuti akandisiyire kwathu?”<br />

Atamva zimenezi, mnyamata wamkulu uja anangoti<br />

duu. Koma wamng’ono uja anapinda malaya ake<br />

n’kusenza thumbalo n’kuuza munthu wachikulireyo<br />

kuti, “Tiyenitu muzinditsogolera.” Bamboyo<br />

anangomwetulira n’kumuuza kuti, “Tenga thumbali<br />

mwana wanga, ndakupatsa kuti likhale lako.<br />

Utengenso zonse zimene zili mkatimo.” Mnyamatayo<br />

atamva zimenezo anati, “Ayi, musatero, ndikungofuna<br />

kukuthandizani basi.” Koma bamboyo anamuuza kuti<br />

wamupatsa monga mphatso. Mnyamatayo atatsegula<br />

thumbalo, sanakhulupirire zimene anaona. Anapeza<br />

kuti thumbalo linali lodzadza ndi miyala yamtengo<br />

wapatali!<br />

Phunziro: Khalidwe labwino ndi limene limapangitsa<br />

munthu kupeza mwayi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

189


Mafunso<br />

1. Kodi anyamata awiriwa ankafuna chiyani?<br />

2. Kodi anyamatawa anali osiyana bwanji?<br />

3. Ndi uti amene anali wakhalidwe labwino?<br />

N’chifukwa chiyani mukutero?<br />

4. Kodi khalidwe labwino linathandiza bwanji<br />

mnyamata wamng’ono uja kupeza mwayi<br />

waukulu?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

190


Chisoni Chinapha Nkhwali<br />

Kalekalelo Njoka inkafuna kuwoloka mtsinje wina.<br />

Ndiye popeza palibe chimene ikanachita kuti iwoloke<br />

yokha, inapempha Nkhwali kuti aithandize. Nkhwaliyo<br />

inamva chisoni zedi ndi mmene Njokayo inkaonekera<br />

ndipo inavomera kuti ichitadi zimene Njokayo<br />

inkafuna. Inauza Njokayo kuti, “Zizengereze m’khosi<br />

mwangamu!” Kenako inanyamuka n’kuuluka. Itafika<br />

kutsidya, Nkhwaliyo inauza Njokayo kuti, “Bwanawe,<br />

tafikatu. Tsopano ukhoza kutsika kuti uzipita.” Koma<br />

Njokayo inakana kwamtuwagalu kuti sichoka.<br />

Pamapeto pake, chisoni chinachitsa kuti Nkhwali ione<br />

tsoka la nkhuku.<br />

Phunziro: Chisoni nthawi zina chimapweteketsa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

191


Mafunso<br />

1. N’chiyani chinachititsa kuti njoka ipemphe<br />

thandizo kwa nkhwali<br />

2. Kodi njokayo inayamikira zimene mnzakeyo<br />

anamuchitira?<br />

3. N’chifukwa chiyani tinganene kuti nkhwali<br />

sinaganize bwino povomera kuthandiza njoka?<br />

4. Kodi nkhwali inakumana ndi zotani pamapeto<br />

pake?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

192


Chisoni Chinaphetsa Wosema Mitondo<br />

Nthawi ina alenje anavumbulutsa gondwa ndipo<br />

anayamba kumuthamangitsa. Alenjewo<br />

anamupezeketsa gondwayo moti anangotsala pang’ono<br />

kumugwira. Gondwayo anayesetsa kukoka phazi<br />

koma sizinam’thandize moti anaganiza zopempha<br />

thandizo kwa munthu wina yemwe ankasema mitondo<br />

m’nkhalangomo. Atatoperatu, gondwayo anapempha<br />

wosema mitondoyo kuti, “Ndithandizeni chonde<br />

ndagwira mwendo wanu. Alenjewa akufuna moyo<br />

wanga, chonde ndipulumutseni!” Wosema mitondoyo<br />

anamva chisoni kwambiri ndipo anauza Gondwayo<br />

kuti amubisa. Koma popeza panalibe malo pafupi<br />

pomwe akanamubisapo, wosema mitondoyo<br />

anangoganiza zomubisa m’kamwa. Alenjewo atafika<br />

anafunsa wosema mitondoyo kuti, “Mwaona Gondwa<br />

atadutsa apa?” Koma wosema mitondoyo anapukusa<br />

mutu posonyeza kuti sanamuone. Ndiyeno alenjewo<br />

atachoka, munthuyo anauza Gondwa uja kuti, “Alenje<br />

ajatu apita, ukhoza kutuluka tsopano!” Koma<br />

gondwayo anayankha kuti, “Tadikirani kaye pang’ono,<br />

muli kenakake kokoma muno!”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

193


Phunziro: Kumaona anthu owathandiza, ena akhoza<br />

kungokubweretsera mavuto.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani wosema mitondo anaganiza<br />

zothandiza Gondwa?<br />

2. Kodi Gondwa anayamikira zimene munthuyo<br />

anamuchitira?<br />

3. Mukuganiza kuti chinamuchitikira munthuyu<br />

n’chiyani?<br />

4. Kodi nthanoyi ikufanana bwanji ndi ya mutu<br />

wakuti, “Chisoni Chinaphetsa Nkhwali”?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

194


Azimayi Anzeru<br />

Kalekalelo, mfumu ina yamphamvu kwambiri inalanda<br />

mzinda wina. Mfumuyi inalamula kuti amuna onse a<br />

m’mudziwo aphedwe, koma akazi anauzidwa kuti<br />

akhoza kuthawa. Anauzidwanso kuti akhoza kutenga<br />

chilichonse chimene angakwanitse kunyamula.<br />

Azimayiwa atamva izi, anangolowa m’nyumba zawo<br />

n’kukaika amuna awo kumbuyo n’kumathawa nawo.<br />

Mfumuyo itaona zimenezi inafunsa azimayiwo kuti,<br />

“N’chifukwa chiyani mukuchita zimenezi? Si paja<br />

ndinakuuzani kuti muthawe nokha?” Koma azimayiwo<br />

anayankha kuti, “Pajatu munati tikhoza kutenga<br />

chilichonse chimene tingakwanitse kunyamula! Ndiye<br />

kwa ifeyo katundu ofunika kwambiri ndi amene<br />

tanyamulayu!” Mfumuyo inaona kuti zimenezi<br />

n’zomveka, moti inalola azimayiwo kutenga katundu<br />

ananyamulayo, ndipo amuna onse a m’mudziwo<br />

anapulumuka.<br />

Phunziro: Osamaiwala zinthu zofunika kwambiri.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

195


Mafunso<br />

1. N’chiyani chikusonyeza kuti azimayiwa anali<br />

anzeru?<br />

2. Kodi ndi zinthu zina ziti zimene akanakwanitsa<br />

kunyamula, kupatulapo amuna awo?<br />

3. Kodi anagwiritsa ntchito bwanji mawu a<br />

mfumu kupulumutsa amuna awo?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

196


Mwana Wosamvera<br />

Mayi wina anali ndi mwana wosamvera, mwanayu<br />

sankamva ndi pakamwa pokha, koma am’menye basi.<br />

Nthawi zina amati akamuuza kuti asachite zinazake,<br />

ankakhala ngati wamva, koma zomwe ankachita<br />

pambuyo pake, zinkasonyeza kuti zimene wauzidwazo<br />

zangolowera khutu ili n’kutulukira linalo. Ndiye tsiku<br />

lina mayiyo anauza mwanayo kuti, “Kunjatu kwacha<br />

kalekale, nyamuka uzipita kusukulu, ukachedwatu<br />

aphunzitsi akakubweza!” Koma mwanayo sanamvere<br />

ndipo anapitirizabe kumuuza kambirimbiri, koma ayi<br />

ndithu ankangozikankhira kunkhongo. Ankachita<br />

zinthu ngati kuti kusukuluko ankakaphunzirira mayi<br />

akewo. Koma akakhalanso pakhomo ankawatopetsa<br />

mayi ake chifukwa ankakana kugwira ntchito.<br />

Chinthu chimene ankachidziwa kunali kudya basi.<br />

Ndiye mayiyu atatopa ndi khalidwe la mwanayu,<br />

ananyamuka n’kupita kwa a Chikwapu. Atafika<br />

anawauza kuti, “Mwana wanga akuvuta, kodi<br />

mungakamukwapule kuti apite kusukulu?” Koma a<br />

Chikwapu anakana. Zitatero mayiyo anaganiza zopita<br />

kwa a Moto. Anawafotokozera kuti akufuna kuti a<br />

Motowo akawotche a Chikwapu chifukwa akukana<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

197


kukakwapula mwana, ndipo mwana akukana kupita<br />

kusukulu. Koma nawonso a Moto anakana. Mayiyo<br />

anakhumudwa kwambiri ndi zimenezi moti anaganiza<br />

zopita kwa a Madzi. Atafika kumeneko<br />

anawafotokozera kuti, “Pepanitu a Madzi. Ineyo<br />

ndikufuna thandizo lanu. Ndikufuna mukazimitse a<br />

Moto chifukwa akukana kuwotcha a Chikwapu, a<br />

Chikwapu akukana kukwapula mwana, mwana<br />

akukana kupita kusukulu.” Koma nawonso a Madzi<br />

anakana. Kenako mayiyo anapita kwa a Ng’ombe.<br />

Anawafotokozeranso nkhani yonse koma nawonso<br />

anakana. Zitatero, anaganiza zopita kwa M’busa<br />

wang’ombe. M’busayo anawamvetsa mayiwa chifukwa<br />

nawonso anali ndi mwana wovuta ndipo ananyamuka<br />

n’kuyamba kuthamangitsa a Ng’ombe. A Ng’ombe<br />

ataona kuti zavuta, anayamba kuthamangira kumene<br />

kunali a Madzi. A Madzinso ataona kuti amwedwa,<br />

anaganiza zokazimitsa a Moto. A Moto ataona kuti<br />

azimitsidwa, anaganiza zokawotcha a Chikwapu.<br />

Ndipo a Chikwapu ataona kuti zinthu sizili bwino,<br />

anayamba kukwapula mwana ndipo mwana anapita<br />

kusukulu.<br />

Phunziro: Osamamva nkhwangwa ili m’mutu.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

198


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani mwana ankakana kupita<br />

kusukulu?<br />

2. Kodi zimene ankachitazi zikanakhudza bwanji<br />

tsogolo lake?<br />

3. N’chiyani chinachititsa kuti apite kusukulu?<br />

4. Kodi nkhaniyi ikusonyeza kuti kulanga mwana<br />

n’kofunika bwanji?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

199


Mwana Wamwano<br />

Pamudzi wina panali mwana wosamvera komanso<br />

waulesi. Makolo ake amati akamutuma ankakana, apo<br />

ayi ankangochokapo n’kupita kukabisala. Ndiye tsiku<br />

lina anamukakamiza kuti apite kumunda ndipo<br />

atafika kumundako, mwanayo anakwera mumtengo<br />

n’kubisala. Mumtengomo munali njoka ndipo njokayo<br />

inamuluma moti anafera pompo. Makolo ataona kuti<br />

mwana wawo sakuoneka, anayamba kumufunafuna<br />

ndipo anamupeza pansi pa mtengo atafa. Atayang’ana<br />

mumtengo, anaona njoka ndipo anadziwa kuti ndi<br />

imene yamuluma. Makolowo ataona izi anati, “Mwana<br />

wathuyu wafa chifukwa cha mwano. Akanamvera<br />

zimene tinamuuza, sakanafa!”<br />

Phunziro: Mwana womvera amakhala ndi moyo<br />

wautali.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mwanayu anali ndi mavuto otani?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani<br />

atafika kumunda anakwera mumtengo?<br />

3. Kodi anakumana ndi mavuto otani?<br />

4. Kodi akanatani kuti apewe mavuto amenewa?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

200


Bambo ndi Mwana Wake<br />

Tsiku lina bambo wina anakwera sitima limodzi ndi<br />

mwana wake. Sitimayo itangoyamba kuyenda,<br />

mwanayo anayamba kulongolola m’sitimayo ndipo<br />

amauza bambo ake kuti, “Ababa, taonani mitengo<br />

ikuthamanga! Taonaninso nyumbazi, zikuthamangatu<br />

ngati mphenzi!” Bambo akewo anangogwedezera mutu<br />

n’kumusiya. Anthu ena ataona izi anafunsa bamboyo<br />

kuti, “Kodi mwana wanuyu n’koyamba kukwera<br />

sitima?” Koma bamboyo anapukusa mutu. Kenako<br />

mwana uja anayamba kufuntha m’sitimayo, amati<br />

akaona chinthu, amachiyandikira kuti achionetsetse<br />

ndipo anthu ena anayamba kusowa naye mtendere.<br />

Ndiyeno munthu wina anauza bambo a mwanayo kuti,<br />

“Kodi mwana wanuyu mutu wake umagwira?<br />

N’chifukwa chiyani akungokhala ngati anadya matako<br />

a galu?” Ndiyeno bamboyo anayankha kuti, “Si bwino<br />

kupupuluma kuweruza munthu wina usakudziwa<br />

nkhani yonse. Pali mawu akuti, ‘osamaweruza<br />

munthu kuchokera pamene iweyo waima, koma<br />

kuchokera pamene munthuyo waima.’ Mawuwa<br />

amatanthauza kuti kumakhala kulakwa kumaweruza<br />

munthu pongotengera zimene ukuona. Pepani kuti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

201


mwana wangayu akukusowetsani mtendere, koma<br />

ineyo ndikumumvetsa. Mwanayutu anabadwa<br />

wosaona. Kuteroko panopa tikuchokera kuchipatala<br />

komwe anakamuchita opaleshoni ya maso moti<br />

wangoyamba kumene kuona. Chilichonse ndi<br />

chachilendo kwa iyeyu moti n’chifukwa chake<br />

akumangodabwa ndi chilichonse. N’chifukwa<br />

chakenso ineyo sindinamuletse. Ndimaona kuti<br />

akatopa asiya yekha.” Atamva zimenezi, anthuwo<br />

anamumvetsa moti anangogwira pakamwa.<br />

Phunziro: Osamafulumira kuweruza ena usakudziwa<br />

nkhani yonse.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi vuto la mwanayu linali chiyani?<br />

2. Kodi tinganene kuti mitengo yomwe ankaona<br />

inkathamangadi?<br />

3. N’chifukwa chiyani anthu ena anayamba<br />

kudabwa naye?<br />

4. Kodi pamene bamboyo anagwedezera mutu<br />

ankatanthauza chiyani? Nanga bwanji pamene<br />

anapukusa mutu?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

202


5. Kodi tinganene kuti anthu a m’sitima ija<br />

analakwitsa kuganiza kuti mutu wa mwanayo<br />

sugwira?<br />

6. Kodi mukuganiza kuti akanatani kuti adziwe<br />

vuto la mwanayo popanda kunena zachipongwe?<br />

7. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

203


Kupulumukira M’kamwa mwa Mbuzi<br />

Tsiku lina anyamata awiri anapeza mbuzi<br />

itamangidwa pamtengo wina ndipo anaganiza zoti<br />

aibe. Atangoyamba kumasula chingwe cha mbuziyo,<br />

mwini wake anabwera ndipo anawafunsa kuti,<br />

“N’chifukwa chiyani mukumasula mbuzi yanga?”<br />

Anthuwo anayamba kuchita mantha. Koma m’modzi<br />

anati, “Tinaona kuti pano palibe msipu wabwino,<br />

ndiye tinaganiza zoti tikaimangirire pamtengo uwo.<br />

Taonani msipu wake ukungoti biriwiribiriwiri,<br />

kukongola. Zoona mbuziyi ife ndi njala msipu uli<br />

m’khonde?” Mwini mbuziyo atamva zimenezi<br />

anawakhulupiriradi. Koma mbuziyo inkadziwa kuti<br />

anthuwo akunama. Ndiye chifukwa choti sitha<br />

kuyankhula, akubawo anapulumukira m’kamwa mwa<br />

mbuzi.<br />

Phunziro: Anthu ena amapulumuka chifukwa cha<br />

bodza.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

204


Mafunso<br />

1. Kodi cholinga cha anyamatawa chinali chiyani?<br />

2. Kodi ankanena zoona pamene ananena kuti<br />

amafuna kumangirira mbuziyo pamene panali<br />

msipu wabwino?<br />

3. Kodi anyamatawa anapulumukira pati?<br />

4. Tiyerekeze kuti munthu wina wapulumuka<br />

mwamwayi galimoto ikufuna kumugunda, kodi<br />

kungakhale kulondola titanena kuti wapulumukira<br />

m’kamwa mwa mbuzi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

205


Kodi Wochimwa Anali Ndani?<br />

Pa nthawi ina alimi 10 anali paulendo. Ali paulendowo<br />

kunayamba chimvula champhamvu komanso cha<br />

ziphaliwali. Alimiwo ataona kuti mvulayo ikhoza<br />

kuwapweteka, anaganiza zobisala m’kanyumba kena.<br />

Koma atafika m’kanyumbako, anaona kuti<br />

chiphaliwali china chinkangozungulira kanyumbako.<br />

Pamalopo panali chiphokoso choswa makutu, moti<br />

alimiwo anayamba kunjenjemera. Kenako anayamba<br />

kuganiza kuti n’kutheka zoti pakati pawo pali munthu<br />

wina wochimwa kwambiri, yemwe chiphaliwalicho<br />

chikufuna kuti chimuphe. Ndiye anaganiza zopeza<br />

munthuyo kuti amutulutse panja n’cholinga choti<br />

chiphaliwalicho chikamusasanthe. Anachita zimenezi<br />

chifukwa samafuna kuti chiphaliwalicho chiphetse<br />

anthu osalakwa. Alimowo anakambirana zoti akoleke<br />

zisoti zawo pamalo enaake ndipo munthu amene<br />

chisoti chake chitauluke ndi mphepo, ndi amene ali<br />

wochimwa. Atachita zimenezi, chisoti cha mlimi wina<br />

chinauluka ndipo alimi enawo atangoona zimenezi,<br />

anamugwira n’kumuponyera panja mopanda chifundo<br />

m’pang’ono pomwe. Koma munthuyo atangotuluka<br />

panja, chiphaliwalicho chinasiya kuzungulira<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

206


kanyumbako ndipo chinamenya denga la kanyumbako<br />

moopsa kwambiri moti alimi 9 anatsala aja anafera<br />

momwemo. Pamenepa m’pamene zinadziwika kuti,<br />

mlimi anamutulutsa uja ndi amene anali wabwino,<br />

ndipo chifukwa cha munthuyo chiphaliwalicho<br />

chinkangozungulira nyumbayo osaiomba. Ndiye<br />

pamene alimi 9 otsala aja anatulutsa mlimiyu,<br />

chiphaliwalicho chinaona kuti mpulumutsi wawo<br />

wachoka, ndipo chinalanga alimi oipa mtimawo mwa<br />

kuwapha. Chinawalanga chifukwa anatulutsa mnzawo<br />

paja, osamuchitira chifundo ngakhale pang’ono.<br />

Phunziro: Usanayambe kuloza kuipa kwa munthu<br />

wina, kumayamba kaye wayeza kuipa kwako.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

207


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani alimiwa anaganiza kuti<br />

pakati pawo pali munthu wina wochimwa amene<br />

chiphaliwalicho chinkamufuna?<br />

2. Kodi atamugwira n’kumuponyera panja<br />

chinachitika n’chiyani?<br />

3. Kodi tinganene kuti wochimwa anali ndani<br />

kwenikweni?<br />

4. Kodi mukunganiza kuti chikanachitika<br />

n’chiyani, akanamulola mlimiyu kukhalabe nawo<br />

limodzi?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

208


Mtsuko Wochucha Ndalama<br />

Kalekalelo kunali munthu wina wochakachika, yemwe<br />

anapeza mtsuko waukulu m’munda mwake. Kenako<br />

anayamba kuukumba ndipo atatero anautenga<br />

n’kupita nawo kunyumba kwake. Atafika anauza<br />

mkazi wake kuti autsuke. Koma mkazi wakeyo<br />

atangotsiramo sopo, mtsukowo unayamba kuchucha<br />

sopo wambirimbiri. Amati akakhuthula sopoyo, sopo<br />

winanso amatuluka n’kudzaza mtsukowo. Bamboyo<br />

anayamba kugulitsa sopoyo ndipo mtsukowo<br />

unapitirizabe kutuluka sopo wambiri moti bamboyo<br />

ankapeza ndalama zosaneneka. Koma tsiku lina,<br />

mwangozi, ndalama inagwera mumtsuko uja ndipo<br />

mtsukowo unasiya kuchucha sopo n’kuyamba<br />

kutuluka ndalama. Amati akazichotsamo, zina<br />

zimatulukanso, moti banjali linakhala ndi ndalama<br />

zankhaninkhani, n’kulemera. Ndiye munthuyo anali<br />

ndi bambo ake okalamba kwambiri, womwe ankakhala<br />

kumudzi wina. Bambo akewo analibiretu mphamvu<br />

zoti angadzisamalire, moti mwana wawoyo anawatenga<br />

n’kumakhala nawo. Koma atakhala kwa kanthawi,<br />

munthuyu anayamba kuona kuti bambo akewo ndi<br />

aulesi moti anawauza kuti azigwira ntchito yochotsa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

209


ndalama mumtsuko uja. Koma chifukwa cha<br />

ukalamba, bambowo zinkawavuta kuchita zimenezi<br />

ndipo mwana wawoyo anapsa mtima n’kuyamba<br />

kuwalalatira amvekere, “Ndinu munthu wamanja<br />

lende. N’chifukwa chiyani mukulephera kugwira<br />

ntchito yophwekayi? Pakhomo panotu timayendera<br />

mawu akuti wosagwira ntchito asadye. Ndiye ngati<br />

simukufuna kugwira ntchito, mudziwa chochita.”<br />

Zitatere gogoyo anakhumudwa kwambiri poona kuti<br />

mwana wake weniweni wayamba kumunyoza chifukwa<br />

choti ndi wopeza bwino. Kenako anangotembenuka ali<br />

pintchapintcha kuti atuluke panja. Koma atangotero,<br />

anapunthwa n’kugwera mumtsuko muja ndipo<br />

anafera momwemo. Nthawi yomweyo mtsuko uja<br />

unayamba kutulutsa mitembo yambirimbiri. Amati<br />

akachotsa ina, inkatulukanso ina. Ndalama zonse<br />

zomwe zinatuluka mumtsuko uja zinathera kuika<br />

maliro a bambo ake ndipo ankati akaika lero maliro,<br />

mawanso amakaika ena. Kenako munthuyo anafika<br />

potopa ndi kuika maliro a bambo akewo, moti anaswa<br />

mphikawo ndipo pamene ankauswa n’kuti ali<br />

kwakwatuke wotheratu, wosowa ndi ya mchere<br />

yomwe.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

210


Phunziro: Ukakhala pabwino, usamanyoze ena.<br />

Mafunso<br />

1. N’chiyani chinathandiza munthu wotchulidwa<br />

m’nkhaniyi kutuluka mu umphawi?<br />

2. Kodi anatani atazindikira kuti bambo ake<br />

sangakwanitse kudzisamalira okha?<br />

3. N’chifukwa chiyani anakwiya ataona kuti<br />

bambo akewo amalephera kuchotsa ndalama<br />

mumtsuko uja?<br />

4. Kodi mapeto ake anali otani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

211


Mphamvu Zobwereka<br />

Nthawi inayake, Nkhandwe inakumana ndi Kambuku.<br />

Kambukuyo atangomuona anatulutsa dzimano zake,<br />

n’kutulutsa zala zake n’kuyamba kuthamangira kunali<br />

Nkhandwe kuja kuti aidye. Koma Nkhandweyo inati,<br />

“Pepani achimwene, taimani kaye! Osamafulumira<br />

kuganiza kuti m’nkhalango muno amphamvu ndinu<br />

nokha. Mphamvu zanutu zikulenga, tikaziyerekeza ndi<br />

zanga. Tiyeni tiyendere limodzi, ndipo inuyo<br />

muziyenda pambuyo panga. Anthu akandiona ineyo<br />

koma osachita mantha, inuyo mundidye. Koma<br />

akandiona n’kuchita mantha, basi mundileke.”<br />

Kambukuyo anagwirizana ndi zimenezi ndipo<br />

Nkhandweyo inayamba kuyenda kulowera<br />

kwinakwake, Kambukuyo akutsatira pambuyo.<br />

Kenako anakumana ndi gulu la anthu ndipo ataona<br />

kuti kukubwera Nkhandwe, koma kumbuyo kwake<br />

kuli Kambuku, nthawi yomweyo analiyatsa liwiro la<br />

mtondo wadooka. Kenako Nkhandwe ija inati,<br />

“Waonatu, ndinali patsogolo ndine, koma anthu<br />

atandiona anachita mantha kwambiri moti<br />

anangotsala pang’ono kudziipitsira!” Kambukuyo<br />

ataona zimenezi anaona kuti mnzakeyodi ndi patali,<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

212


moti ananyamuka n’kuyamba kuthawa. Ankaganiza<br />

kuti anthu aja amathawadi Nkhandweyo, osadziwa<br />

kuti mphamvu zake zinali zochita kubwereka.<br />

Nkhandweyo inali itabwereka mphamvu za<br />

Kambukuyo, yemwe anthu aja anamuona akubwera<br />

pambuyo pake.<br />

Phunziro: Osamaopa mphamvu zochita kubwereka.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Nkhandwe inachita chiyani pofuna<br />

kudzipulumutsa?<br />

2. Kodi anthu aja ankathawa chiyani<br />

kwenikweni?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

213


Anzeru Omwe Anali ndi Vuto Losaona<br />

Kalelo kunali anthu ena asanu ndi awiri omwe anali<br />

ndi vuto losaona. Anthuwa anali anzeru kwambiri moti<br />

anthu ankawatayira katsatsa akamva zimene<br />

zinkatuluka pakamwa pawo. Ndiye tsiku lina anthuwa<br />

anaganiza zopita kumalo ena kuti akaone zinyama.<br />

Atafika kumeneko, anapita pamene panali njovu.<br />

Anthu anayi anagwira miyendo ya njovuyo, m’modzi<br />

anagwira chimulomo cha njovuyo, wina anagwira<br />

pamimba ndipo wina anagwira mchira. Ndiye yemwe<br />

anagwira chimulomo uja anayamba kuuza anzakewo<br />

kuti, “Ine ndiganiza kuti njovu imaoneka ngati njoka.”<br />

Koma mnzake amene anagwira kumchira uja<br />

anamutsutsa n’kunena kuti, “Iyayi, imaoneka ngati<br />

chingwe.” Ena amene anagwira miyendo aja<br />

anagwirizana chifukwa anati, “Nonsenu mukunama,<br />

njovu imaoneka ngati mtengo.” Koma amene anagwira<br />

pamimba uja anayamba kunena anzakewo kuti ndi<br />

wopanda nzeru ndipo anati, “Nonsenu ndi a ziwala<br />

m’maso, njovutu imaoneka ngati phiri.” Kenako anthu<br />

onsewo anayamba kukangana moti zinthu zinafika<br />

poipa kwambiri. Munthu wina yemwe ankangoonerera<br />

zimene zinkachitikazo anafika pamalowo ndipo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

214


anawauza kuti, “Aliyense wa inu wangogwira mbali<br />

imodzi ya njovuyi, moti mukanaphatikiza zomwe<br />

nonsenu mukudziwa, mukanatha kudziwa kuti njovu<br />

yonse imaoneka bwanji.”<br />

Phunziro: Palibe amadziwa zonse.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani anthuwa ankatsutsana?<br />

2. Kodi onsewo ankanama?<br />

3. Kodi akanatani kuti adziwe mmene njovu<br />

imaonekera?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

215


Nkhuku ndi Nkhunda<br />

Kunyumba kwina kunabwera alendo mwadzidzidzi.<br />

Ndiyeno paja kulandira alendo kumaonekera m’mbale,<br />

anthu a pakhomopo anaganiza zowaphikira nsima.<br />

Ndiye popeza anali ndi Nkhunda komanso Nkhuku,<br />

anayamba kukambirana kuti aphe chiyani. Ena ankati<br />

aphe Nkhuku pomwe ena ankati aphe Nkhunda.<br />

Nkhuku itamva zimenezi inayamba kukuwa kuti,<br />

“Koma nkhundayooooo!” Ndipo Nkhunda inkati,<br />

“Mulungu ngwamkulu, Mulungu ngwamkulu,<br />

Mulungu ngwamkulu!” Nkhuku ija inkasokosa<br />

kwambiri moti anthu aja anaiona. Ndiyeno wina anati,<br />

“Bwanji tiphe Nkhuku, chifukwa tikapha Nkhunda,<br />

tipha zambiri.” Nkhukuyo inapitirizabe kukuwa kuti,<br />

“Koma nkhundayooooo!” Ndiye basitu, anthu aja<br />

anayamba kuthamangitsa Nkhuku ija ndipo ataigwira<br />

anaipha, moti maliro ake, alendo aja anadyera nsima.<br />

Phunziro: Osamakankhira anzako mavuto, chifukwa<br />

zimatha kutembenuka.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

216


Mafunso<br />

1. Kodi zimene Nkhuku ndi zimene Nkhunda<br />

imanena m’nkhaniyi kutabwera alendo zikufanana<br />

ndi mmene zenizeni zimalirira?<br />

2. N’chifukwa chiyani eni khomo anaganiza zopha<br />

Nkhuku?<br />

3. Kodi Nkhuku inakankhira bwanji makala<br />

pamalaya a mnzake?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

217


Mankhwala a Banja<br />

M’mudzi wina munali mayi wina, yemwe nthawi zonse<br />

ankangokhalira kudandaula kuti banja lake<br />

silikuyenda bwino. Ankasirira kwambiri akaona<br />

anzake amene anakwatira ndi kumbuyo komwe,<br />

akusangalala ndi mabanja awo. Banja lake linali ndi<br />

vuto limodzi. Mwamuna wake ankangokhalira<br />

kumukutumula ndipo iye ankaona kuti amayesetsa<br />

kumusamalira komanso kuchita zonse zofunika.<br />

Ankati akapita kwa alangizi, ankangomuuza kuti,<br />

“Banjatu n’kupirira, ndiye kaya mwamuna wanu<br />

akumakukunthani, muzingopirira basi. Banja ndiye<br />

limenelo!” Ndiye atatopa ndi nkhanza zimene<br />

mwamuna wake ankamuchitira, anaganiza zopita kwa<br />

munthu wina wodziwa zitsamba kuti akamupatse<br />

mankhwala achikondi. Atafika kwa munthuyo,<br />

anamufotokezera zonse ndipo munthuyo<br />

sanachedwechedwe koma kulowa m’tchire<br />

n’kukathyola kamtengo kenakake. Anamupatsa<br />

mayiyo n’kumuuza kuti, “Mukakakangofika<br />

kunyumba kwanu, musakayankhule chilichonse.<br />

Mukangoika kamtengo aka m’kamwa mwanu<br />

n’kukhala chete. Musakayerekeze kutsegula<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

218


pakamwa, chifukwa mukakatero, mankhwalawa<br />

akasuluka.” Mayiyo anauyambadi wakwawo ndipo<br />

atafika anatsatira malangizo anapatsidwa aja.<br />

Mwamuna wake atabwera, anamuphikira nsima<br />

n’kukamupatsa, ndipo mwamunayo anati,<br />

“Ndinakuuza kuti ndili ndi njala?” Mkaziyo atamva<br />

mawu osayamikawo anapsa mtima kwambiri, koma<br />

chifukwa choti anauzidwa kuti asatsegule pakamwa,<br />

sanayankhe chilichonse. Mwamuna uja anadabwa<br />

kwambiri ndi zimenezi, moti anangotenga nsimayo<br />

n’kuyamba kudya. Kungoyambira tsiku limenelo<br />

mwamuna wakeyo sanamumenyenso ndipo patapita<br />

masiku angapo, mayiyo anapitanso kwa munthu<br />

wazitsamba uja kuti akamuthokoze, ndipo<br />

anamufotokozera kuti mankhwala anamupatsa aja<br />

akuthandizadi. Koma munthuyo anati, “Sikuti ndi<br />

mankhwalawo amene akukuthandizani. Ndi mtengo<br />

wachabechabe womwe ndinathyola m’thengomo. Vuto<br />

lanu mayi ndi kulongolola! Mpofunika muphunzire<br />

kuweta lilime lanulo.”<br />

Phunziro: Mavuto ambiri amene timakumana nawo<br />

amayamba chifukwa cha pakamwa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

219


Mafunso<br />

1. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani banja la<br />

mayiyu silinkayenda bwino?<br />

2. Kodi vuto la mayiyu linali chiyani?<br />

3. Kodi mankhwala amene munthu wodziwa<br />

zitsamba uja anamupatsa ndi amene anathandiza<br />

kuti banja lake liziyenda bwino?<br />

4. N’chifukwa chiyani tiyenera kusamala ndi<br />

pakamwa pathu?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

220


“Ndifera Manyazi Mkazi Wanga”<br />

Tsiku lina Aphiri anauza akazi awo kuti, “Mkazi<br />

wanga, zinthu ndiye zativuta. Tipange bwanji kuti<br />

tipeze ufa? Sindingalole kuti ana angawa afe ndi njala<br />

ine ndikuona. Koma ndisanameyi, palibe chimene<br />

ndikuona kuti ndingachite.” Kenako anapukusa mutu<br />

wopanda nyanga. Mkazi wakeyo anavomerezadi<br />

zimene mwamuna wake ananena ndipo<br />

anawalimbikitsa kuti asadandaule. Kenako<br />

mwamunayo anati, “Mkazi wanga, ndaganiza pulani.<br />

Bwanji ineyo ndinyengezere kumwalira? Ndiye uike<br />

mbale pamsewupo. Anthu akamaponya ndalama<br />

zachipepeso, iweyo uzipita kukazichotsamo<br />

n’kukazibisa.” Koma mkaziyo anafunsa mwamuna<br />

wakeyo kuti, “Nanga bwanji anthu akayamba kubwera<br />

pakhomo pano? Kodi ndiwauza chiyani akanena kuti<br />

akupititseni kumotchale? Mukafa ndi kuziziratu inu?”<br />

Bamboyo anati, “Usadandaule ndi zimenezo, ineyo<br />

ndichita zinthu zoti asazindikire kuti ndili moyo. Koma<br />

akanena kuti andipititse kumotchale, iweyo ukane.<br />

Ungowonetsetsa kuti ndalama zomwe zikuponyedwa<br />

m’mbale zikuyenda bwanji. Ineyo ndidzuka mawa<br />

anthu asanaganize zotulutsa maliro panja.”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

221


Mkaziyo anagwirizana ndi maganizowo ndipo<br />

mwamunayo ananamiziradi kumwalira ndipo mkazi<br />

wakeyo anayamba kulira. Mbale inaikidwadi pamsewu<br />

ndipo anthu anayamba kuponyamo. Posakhalitsa<br />

anthu ena anayamba kuyenda m’midzi n’kumatolera<br />

ufa, nkhuni komanso ndalama ndipo akabwera nazo<br />

ankazipereka kwa mayi uja. Ndiyeno m’mawa kutacha,<br />

anthu anayamba kubwera ndipo ena anakagula<br />

bokosi n’kunyamula Aphiri n’kuwaikamo. Koma<br />

atawaika m’bokosimo, Aphiri tulo tidawatenga.<br />

Mkazi uja ankayembekezera kuti mwamuna wake<br />

adzuka. Koma ataona kuti sakudzuka, anapita pafupi<br />

ndi bokosilo n’kuyamba kulira amvekere, “Inu bambo<br />

a Pofera tadzukani chondeeee! Tadzukani inuuu!<br />

Ndimayesa munati mudzuka inu!” Azimayi anabwera<br />

kudzatonthoza mnzawoyo poganiza kuti chisoni<br />

chamugwira. Pamene bamboyo ankadzuka n’kuti<br />

pakhomopo pali namtindi wa anthu ndipo Aphiri<br />

atamva phokoso la anthuwo komanso nyimbo<br />

zachisoni zikuimbidwa, anachita manyazi kuti adzuke.<br />

Mkazi wawo uja anapitirizabe kulira mouza mwamuna<br />

wakeyo kuti adzuke, koma Aphiri anangoti zii. Amati<br />

akamva mkazi wawoyo akulira ankangonena<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

222


chapansipansi kuti, “Ndifera manyazi mkazi wanga!”<br />

Posakhalitsa kunabwera adzukulu kuchokera<br />

kumanda ndipo anatenga misomali n’kuyamba<br />

kukhoma bokosilo. Amati akati khoo! Mayi uja amalira<br />

mosatonthozeka, “Amunanga inu dzukani, chonde<br />

tadzukani. Nditani nawo ine anawa?” Kenako<br />

anakhomanso wina kuti khoo mpaka anamaliza.<br />

Anthu ankangoganiza kuti mayiyo akuyankhula<br />

zimenezo chifukwa cha chisoni, osadziwa kuti<br />

akunena nkhaninkhani. Pamapeto pake anthu<br />

ananyamula bokosi lija ndipo Aphiri anakaikidwa<br />

m’manda chifukwa cha manyazi.<br />

Phunziro: Osalola kulowa m’mavuto chifukwa cha<br />

manyazi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

223


Mafunso<br />

1. Kodi Aphiri ataona kuti zinthu zavuta<br />

panyumba pawo anapanga pulani yotani?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti anawerengera mtengo<br />

wake?<br />

3. N’chifukwa chiyani Aphiri ankachita manyazi<br />

kudzuka?<br />

4. N’chifukwa chiyani anthu sanadabwe ndi<br />

mawu amene akazi a Aphiri ankanena akamalira?<br />

5. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

224


Atambwali Sametana<br />

M’mudzi wina munali atsinzina n’tole awiri. Wina<br />

dzina lake linali Paguza ndipo wina anali Saguza.<br />

Tsiku lina Paguza anatenga thumba la mpunga<br />

n’kuikamo mchenga ndipo pamwamba pa mchengawo<br />

anaikapo mpunga n’cholinga choti thumbalo lizikhala<br />

ngati lodzadza mpunga okhaokha. Nayenso Saguza<br />

anatenga mtsuko n’kuthiramo madzi ndipo<br />

pamwamba pamadziwo anathirapo mafuta. Madziwo<br />

ankangoti ndengundengu ngati mafuta ndipo<br />

anasenza mtsukowo n’kumapita nawo kumsika.<br />

Atafika kumeneko, atambwaliwa anakumana ndipo<br />

anagwirizana kuti angosinthana zinthuzo. Paguza<br />

anauza mnzakeyo kuti, “Uwu ndi mpunga<br />

wopunthapuntha, wabwino kwambiri moti<br />

simungapezenso wina yemwe angakugulitseni mpunga<br />

ngati umenewu. Mukakauphika uzikangotuluka<br />

umodziumodzi.” Saguza atamva zimenezo anaona kuti<br />

wapeza munthu watulo, moti sanachedwe koma<br />

kuvomera zoti asinthane ndi mnzakeyo mtsuko<br />

wamafuta. Aliyense anangosenza katundu anapatayo<br />

n’kuuyamba wakwawo. Koma atafika kunyumba<br />

anazindikira kuti apusitsana. Paguza ataona kuti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

225


mnzakeyo wamugulitsa madzi anayamba<br />

kumusakasaka ndipo atamupeza anamufunsa kuti,<br />

“N’chifukwa chiyani wandipusitsa?” Mnzakeyonso<br />

anamufunsa kuti, “Nanga n’chifukwa chiyani iwe<br />

wandigulitsa mchenga?” Atazindikira kuti zawo<br />

n’zimodzi, anayamba kugwirizana kwambiri. Tsiku lina<br />

anapangana kuti apite kukaba kwa mfumu<br />

yam’mudzimo. Atambwaliwa anamva zoti mwana wa<br />

mfumuyo, yemwe anali kutheba, wabwera ndi<br />

chikwama chodzadza ndalama ndipo wapatsa bambo<br />

ake. Atamva zimenezi mitima yawo inkangoti<br />

dyokodyoko, ndipo anagwirizana kuti akumane pakati<br />

pa usiku n’cholinga choti akasowetse chikwamacho.<br />

Kenako anauyamba wa kunyumba kwa mfumuyo.<br />

Mwamwayi pakhomo la mfumuyi panalibe zifuyo<br />

zaukali, moti Paguza anakwanitsa kulowa m’nyumba<br />

ya mfumuyo aliyense osadziwa. Kenako anayenda<br />

monyang’ama n’kukanyamula chikwama chachikulu<br />

chomwe chinali kumutu kwa mfumu yomwe inali<br />

tapatapa ndi tulo. Ndiyeno anafika nacho pazenera la<br />

nyumbayo n’kupatsira Saguza, yemwe anaima panja<br />

pa nyumbayo. Saguza atangolandira chikwamacho<br />

anayamba kuthawa nacho. Atafika kunyumba kwawo,<br />

anasonkhanitsa mudzi wonse ndipo anauza anthu a<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

226


pakwawopo kuti ali ndi chikwama chodzadza<br />

ndalama. Koma anawauzanso kuti, “Pali vuto limodzi.<br />

Munthu winawake akundilondalonda. Akufuna<br />

atatenga chikwamachi.” Anapitiriza kunena kuti,<br />

“Ndalamazi zikhoza kupangitsa kuti aliyense pamudzi<br />

pano akhale mponda makwacha. Ndiye mulola kuti<br />

munthu ameneyu atenge ndalamazi?” Anthuwo<br />

atamva zimenezi anapukusa mitu yawo n’kunena kuti,<br />

“Ayi.” Ndiyeno Saguza anati, “Ndikufuna kuti tibise<br />

chikwamachi, Paguza akabwera, mudzamuuze kuti<br />

ndamwalira.” Anthuwo anagwirizana nazo zimenezo<br />

ndipo posakhalitsa anthu anayamba kubuma<br />

amvekere, “Mayi wawaye, tilowera kuti ife, achimwene<br />

athu atsogolaa.” Pakhomopo panayamba kumveka<br />

chiphokoso chachikulu ndipo posapita nthawi<br />

panyumbapo panadzaza anthu. Ndiyeno m’mawa<br />

kutacha, Paguza anatulukira ndipo anafunsa anthu a<br />

pakhomopo kuti, “Wamwalira ndi ndani?” Anthuwo<br />

anamuyankha kuti, “Mnzanu ujatu anatipeza<br />

m’bandakucha ndipo amanena kuti sakumva bwino<br />

moti anatikomokera m’manja, basitu ulendo unali<br />

womwewo.” Koma Paguza atamva zimenezi anayamba<br />

kukayikira ndipo anati, “Anthuwa akundiuza kuti<br />

Saguza wamwalira. Amwalira bwanji atathawa ndi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

227


chikwama chandalama. Akufuna kundiyenda pansi<br />

ameneyu!” Kenako anauza anthu a pakhomopo kuti,<br />

“Ndingakaone mtembo wake?” Anthuwo anamutengadi<br />

n’kumulowetsa m’chipinda chimene munali<br />

mtembowo. Kenako anayamba kuyankhula ndi<br />

mnzakeyo kuti, “Bwanawe, dzuka kuti tingokambirana<br />

bwinobwino?” Koma mnzakeyo anangoti zii. Kenako<br />

Paguza anauza azimayi ena kuti, “Nditerekereni madzi,<br />

awire ngati ososolera nkhuku.” Azimayiwo anachitadi<br />

zimenezo, mosadziwa kuti akufuna achite nawo<br />

chiyani. Madziwo atabwadamuka, azimayiwo<br />

anawatenga n’kupita nawo kwa Paguza. Paguza<br />

analandira madziwo n’kupempha kapu yake<br />

yotungira. Ndiyeno anayamba kuuza mtembowo kuti,<br />

“Ambwana, dzuka zinthu zisanafike poipa! Koma<br />

mnzakeyo sanayankhe. Kenako anatunga madzi<br />

otentha aja pang’ono, n’kumutsira pamwendo kuti<br />

chwaa! Koma mnzakeyo anapirira ndipo sanatekeseke.<br />

Kenako anatunganso ena n’kumuthiranso kuti chwaa!<br />

koma ayi ndithu Saguza sanasunthe. Ndiyeno Paguza<br />

anati, “Bwanawe, dzuka. Uvulalatu!” Koma Saguza<br />

sanayankhe. Kenako Paguza anati, “Nanga mtembo<br />

umamva kuotcha ngati? Kuti nditsimikizire kuti<br />

mnzangayu wapitadi, ndingomukhuthulira madzi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

228


onsewa.” Ndiyeno anangotenga mtsuko uja<br />

n’kukhuthulira mnzakeyo ndipo Saguza analephera<br />

kupirira. Anadzambatuka kwinaku akulira ndipo<br />

mnzakeyo anati, “Ndinakuuzatu ine, ukanangodzuka<br />

nthawi yomwe ija sukanavutika chonchi.” Pa nthawiyi<br />

n’kuti Saguza atayamba kukupuka m’miyendo ndi<br />

m’mikonomu. Zitatero Paguza ndi Saguza<br />

anagwirizana kuti agawane ndalamazo mofanana,<br />

ndipo anakatenga chikwama chija kuti ayambe<br />

kugawana. Koma atangochitsegula, anapeza kuti<br />

munali mapepala okhaokha.<br />

Phunziro: Utambwali umabweretsa mavuto.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi Paguza ndi Saguza anali anthu otani?<br />

2. N’chifukwa chiyani anayamba kugwirizana?<br />

3. N’chiyani chikusonyeza kuti onsewa anali<br />

adyera?<br />

4. Kodi pali chilichonse chimene anapindula?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

229


Mutu Wodwala Kansire Adatema Kadzidzi<br />

Kalekale pakati pa mbalame zonse, panali kambalame<br />

kena kakang’ono kotchedwa Kansire, enanso amati<br />

Tchala. Kambalameka kankalemekezedwa ndi<br />

mbalame zonse chifukwa mbalamezo zinkati Kansire<br />

ndi mbalame ya ku mizimu, kapena kuti mbalame<br />

yomvana ndi mizimu.<br />

Kansire amati zipatso ndi zakudya zina zikasowa, iye<br />

amaulukira kumanda kotchedwa Makololo n’kuyamba<br />

kulira. Posapita nthawi m’mitengo yonse kumandako<br />

zipatso zimvekere kuti mbwee! kholophethee! Nthambi<br />

za mitengoyo kuti petaa! kulemedwa ndi zipatso<br />

zikuluzikulu.<br />

Tsopano zimati zikatero, phokoso la mbalame<br />

limachita kuti, buu! Panali mbalame ina imene<br />

inkamveka kwambiri ndi phokoso. Mbalameyi inali<br />

yotchedwa Pumbwa. Pokondwerera zipatso zija<br />

mumtengo wa Kachere inkati, “Mbwe, mbwe, bzolo,<br />

bzolo, zanchulukira! zanchulukira!” Tsopano<br />

mbalamezo zikakhuta, zimatera pansi n’kuyamba<br />

kuyamika mbalame ija yotchedwa Kansire.<br />

Kuyamikako inkatsogolera ndi mbalame ija yomveka<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

230


kwambiriyi, Pumbwa. Mbalameyo imati “bzoli! bzoli!<br />

zanchulukira! Ife tiyamika inu Kansire. Lero ife<br />

laponda lamphawi diwa. Tinali padzuwa koma inu<br />

Kansire mwatitoletsa nkhwangwa ndi mpini womwe.<br />

Popanda inu Mfumu Kansire, ife sitikanasambira<br />

m’nkhali monga tachitiramu. Mwa ichi tiyamika,<br />

taphuka chifukwa cha inu mfumu yathu Kansire,”<br />

Anatero Pumbwa poyamika Kansire. “Mawa tibwera<br />

ndi mitolo ya nsembe kuti mupereke kwa mizimu ya<br />

makolo athu,” anatero poyamikira Kansire.<br />

Pumbwa anapitiriza motere, “Pano tikufuna<br />

kukutsimikizirani kuti ndinu mfumu yathu. Enawa<br />

timangowaona chimwendo kong’akong’a, kutalika<br />

chikhosi apoo, kusololokera m’mwamba, koma palibe<br />

chimene adatichitirapo, koma kumangotigogomola ndi<br />

kutinzonzomola pamitu!”<br />

Nthawi yomweyo panamveka mawu ozaza, “Iwe<br />

Pumbwa! thula! Bwanji ukuchitira chipongwe ine?<br />

Kodi kutalika mwendoko ndidakumanani ndine?”<br />

Anatero Nthiwatiwa ali kupalasika ndi ukali, masaya<br />

atatupikana ndi mkwiyo. Mbalame zonse zinangoti<br />

maso pa Nthiwatiwa, yuuu! n’kumangoinyodogola cha<br />

mumtima zili “Ho! Tamuonani gudu wogudukira<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

231


zinthu za eni ake. Tachionani chimwendo kutalika<br />

ngati mitengo ya m’masano.” Mmene zimateromo<br />

zimatunguluza maso, lilime lili pamtunda, milomo<br />

zitapambanitsa kupitiriza kunyodola a Nthiwatiwa aja.<br />

“Ine ndikunenetsa pano!” a Nthiwatiwa anatero,<br />

“Mbalame zonse ndinu opusa kwambiri. Mudzaleka liti<br />

kugodomala kotere? Simungatchule kamwana aka ka<br />

Kansire kuti ndi mfumu. Kodi simukudziwa kuti<br />

mfumu ndine Nthiwatiwa? Kodi n’chilungamo<br />

kumalemekeza Kansire, muleka ife amuna ogona<br />

kukhomo kosatseka? Kodi simudziwa kuti Kansire ndi<br />

nthumbidwa? Kodi Kansire ndi ine titati tipandane<br />

angafe ndani?” Anatero Nthiwatiwa poonetsa kunyada.<br />

“Ndiponi mutalemekezako a Mphungu awo, kaya a<br />

Ng’ongwe awo, a Namng’omba kaya a Namntchichi<br />

awo, kapenanso a Kadzidzi awo chifukwa chokula<br />

mutuwo . . . ”<br />

“Ine ndikuthilira ndemanga mawu amenewo!” anatero<br />

a Namn’gomba, “Mbalame nonsenu muli ndi kaduka<br />

kachinangwa! Si zaulemu kumalemekeza kafinye aka<br />

ka Kansire kamene ife timakatchula kuti kandakhuta<br />

kale ayi!” a Namng’omba anatero powonjezera<br />

ndemanga.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

232


“Zoonadi,” anatero Ng’ongwe ali kutsokomola,<br />

chithokomiro cha pakhosi chili tugwaa! kutupikana<br />

ndi ukali. “Ine ndili kuvomereza Namng’omba.<br />

Kamwana aka ka Kansire sikangakhale mfumu a<br />

Nthiwatiwa ali pompano ayi. Kodi ufumuwo alandirira<br />

chifukwa cha ulosi wokhawokhawo? Kodi chidadza ndi<br />

yani choti munthu akakhala wa kumizimu, wotiitanira<br />

mvula tsono, n’kumatinso yemweyo akhale mfumu?”<br />

anatero Ng’ongwe pofunsa mbalame zonse zija.<br />

Mmenemo n’kuti atawatunguluzira maso ali pamtunda<br />

ngati maso a njoka ija yotchedwa mamba, pam’mero<br />

pali dyokhodyokho chifukwa cha ukali. Mbalame<br />

zonse zija zinangotinso maso pa Ng’ongwe kuti yuu!<br />

“Mwaona nokha palibe woyankha, kutsimikiza kuti<br />

sindikunena zambwerera ayi!” anatero Ng’ongwe.<br />

Nthawi yomweyo Ng’ongwe anapisa mutu wake<br />

mphiko lakumanzere. Potulutsa mutu wake, mbalame<br />

zonse zija zinadodoma poona kuti kukamwa kwake<br />

kunali ndudu ya fodya ili fuubaa! utsi umenewo. Utsi<br />

wina unali kutulukira mphuno.<br />

“Kansire ntchito yake ndi ulosi basi osatinso za ufumu<br />

zizimvekera pa dzina lakenso, izo takana<br />

kwamtuwagalu.” Anatero Ng’ongwe ndudu ija<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

233


atayamba waitula pansi, koma utsi wina ukutulukabe<br />

m’mphuno pamene anali kuyankhula.<br />

“Kambalame kena ngati Pumbwa, kasasokoneze<br />

Kansire ayi. Mulekeni iye azingolingalira njira zabwino<br />

zomvanirana nazo ndi mizimu ya makolo athu amene<br />

adafa kale basi. Amfumu anthu a Nthiwatiwa ndiwo<br />

amene azilinganiza za ufumu wawo monga<br />

zokonzekera za kumeta unamwali pa nthawi<br />

ikubwerayi ya zinamwali za anyamata ndi<br />

asungwana,” anatero Ng’ongwe popumulira<br />

kuyankhula kuja. Ng’ongwe anatolanso ndudu ija ya<br />

fodya, ndiye tsopano kudangooneka kuti, toloooo! Utsi<br />

umenewo mapiko ake ali kuwombetsa m’mimba<br />

kuonetsa ukali, m’menemo n’kuti maso ali psuu! ngati<br />

wopemereredwa ndi utsi kudzenje.<br />

“Chimene tiyenera kumakumbukira n’choti<br />

tisamaiwale sing’anga wathu Mleme kumuitana kuti<br />

nayenso adzadye nawo phwandoli. Taonani ife<br />

zithokomiro zili tugwaa! chimkhuto chimenecho.<br />

Nanga bwanji taiwala ng’anga yathu? Amfumu<br />

Nthiwatiwa akankhe mthenga kwa Mleme kuti abwere<br />

adzadye nawo ufulu talandirawu . . . azimu atigwera<br />

m’mbale . . . atigwera m’mitengo yathuyi kumasano<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

234


kuno,” anateronso Ng’ongwe fodya ali fubafuba utsi uli<br />

kutulukira m’mphuno.<br />

“Wayankhula bwino iwe Ng’ongwe!” anatero<br />

Nthiwatiwa. “Nonsenu musamvere zija amanena<br />

Pumbwa zija ayi. Zija ndi zoyankhula akapasule<br />

okhaokha. Pumbwa sadziwa kuti dziko ndi mafuwa<br />

achita kuchilikiza. Zoyankhula za Pumbwa ndi<br />

zochotsa mafuwa kuti dziko ligwe. Motero, zimene<br />

wayankhula Pumbwa zija aliyense angozithira<br />

kunkhongo. Woyamwa yekhayekha ndi amene<br />

amayankhula zokhuta ngati zimene zija,” Nthiwatiwa<br />

anateronso ali kupenyetsa Pumbwa uja. “Motero tonse<br />

tiyenera kumwazikana koma tonse tidzakumanenso<br />

pano m’mawa dzuwa likutuluka kuti tidzapitirize<br />

kudya madyelerowa.”<br />

M’mawa kutacha dzuwa likutuluka, mbalame zonse<br />

zinali zitasonkhana kale kumasano kuja koma zonse<br />

zinali zitatera pansi zili kwangopenyetsetsa zipatso<br />

m’mitengo muja. Zinali kudikira ulamuliro wa<br />

mbalame ija ya kumizimu yotchedwa Kansire. “Nanga<br />

Kansire ndi Chiuzimbi ali kuti?” Anafunsa motero a<br />

Nthiwatiwa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

235


“Ife sitikudziwa mfumu,” anatero Kadzidzi chimutu<br />

chake chachikulu chija chili nguninguni kugwedezeka,<br />

masaya ali kweevee! ngati wodwala matenda a<br />

kadukutu. “Tonse tabwera, mphachi (kupatula) awiri<br />

mwatamulawo,” anawonjezera motero Kadzidzi.<br />

Dzidzidzi, mbalame zonse zinamva kukwapulitsa kwa<br />

mapiko a mbalame kuti phururu! phururu!<br />

Posakhalitsa zinaona Chiuzimbi akutulukira ali kutera<br />

pansi, Chiuzimbi chachitali ngati chimchira cha<br />

Nkhwere chili vwandaa! Chilinunda ngati cha kunzi ya<br />

ng’ombe chili pholi! pamsana. “Suyo Chiuzimbi uja<br />

mfumu!” anatero Kadzidzi.<br />

“Eya, ndamuona,” Nthiwatiwa anatero.<br />

“Pepani mfumu ndachedwa kufika!” Anatero<br />

Chiuzimbi.”<br />

“Chifukwa?” Nthiwatiwa anafunsa, maso ali psuu!<br />

mutu uli njenjenje ndi ukali.<br />

“Pepani mfumu ndiye kuti . . . ” anangoyamba motero<br />

Chiuzimbi. “Ndiye kuti chiyani? Kodi iwe Chiuzimbi<br />

umanyadira chimthenga chako chachitalichi? Kapena<br />

umanyadira linundali basi n’kumadziyeseza kuti<br />

ndiwe ng’ombe eti? Ife sitingadikire iwe pano<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

236


kutichedwetsa phwando lathuli limene adatipatsa<br />

mlosi wathu Kansire. Kansire pomvana ndi mizimu ya<br />

makolo athu taona m’mitengomu zimene Chisumphi,<br />

kaya Chauta, kaya Mphambe anatipatsa. Kodi<br />

umadziyesa ng’ombe iwe eti?” Anatero Nthiwatiwa<br />

podula pakamwa Chiuzimbi.<br />

“Zachisoni mfumu Kansire wafa?” anatero Chiuzimbi<br />

kuti zonena zake zimveke msanga.<br />

“Ukuti chiyani? Kansire wafa?” Nthiwatiwa anafunsa.<br />

Nthawi yomweyonso panamveka kubuma maliro a<br />

Kansire. Dothi lonse pamalo onsewo linali madzi<br />

khathikhathi ndi misozi yochokera m’maso a mbalame<br />

zija. Nthiwatiwa sanathenso kuyankhula chifukwa cha<br />

phokoso lachisokonezo motere: “Bzolobzolo, bzoii,<br />

mbwembweembwe, gulululu, khurururu, fwakafwaka,<br />

kweeefu, mbirombiro!”<br />

“Nena bwino, ukuti chiyani za Kansire?” Nthiwatiwa<br />

anafunsanso.<br />

“Kansire zoonadi,” anatero Chiuzimbi, “wadwala<br />

pafupi imfa.”<br />

“Khalani chete,” Nthiwatiwa anatero. Chifukwa cha<br />

mawu wotsirizira aja a Chiuzimbi, panali bata kungoti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

237


ziii. “Ndikuti Kansire wadwala pafupi imfa. Usiku<br />

anakomoka katatu.”<br />

“Chabwino, iwe wemwe Chiuzimbi pita kwa sing’anga<br />

wathu Mleme ku Chinsiro ukamuuze za matendawo.<br />

Nonse mubwere pamodzi kuti tonsefe tipitire limodzi<br />

kwa Kansire. Wamva bwino?” anatero Nthiwatiwa.<br />

“Zikomo mfumu,” anatero Chiuzimbi akuuluka kupita<br />

kwa ng’anga ija.<br />

“Zikomooo,” anatero Chiuzimbi.<br />

“Eyaa,” anatero Mleme.<br />

“Koma musavutike n’kundikonzera pokhala ayi.<br />

Ndikhala pachikuni ndatera pano,” Chiuzimbi anatero.<br />

“Kodi n’kwabwino?” Mleme anafunsa.<br />

“Ayi si kwabwino.”<br />

“Chavuta n’chiyani?”<br />

“Matenda kwathuku.”<br />

“Wadwala ndani?”<br />

“A Kumizimu a Kansire.”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

238


“Tsono zikatero n’cho chiyani, atilosere zinthu ndani?”<br />

“Ndimo taonera. Mutu ndithu udawayamba dzana.<br />

Ngakhale amayenda kungoti munthu uja ngolimba.<br />

Mwinanso kuchepa thupi kuwombola. Usiku<br />

anakomoka katatu. Amfumu a Nthiwatiwa atamva ndi<br />

amene anandikankhira nkhongo kunowa, ali basi<br />

muzikabwerera limodzi.”<br />

“Zikomo ndamva. Ine bwenzi n’tabwera ndithu popeza<br />

madzulo ndinalandira mthenga woti kuli phwando,<br />

wosadziwanso kuti n’kumamva zoteronso. Chabwino<br />

dikira pomwepo nditenge lumo lakuthwa loti<br />

tikatemere mankhwala kuti mnzathuyo achire<br />

msanga. Komatu zina leku zina kambu, ine dzinali<br />

ndimangolimva koma titakumana m’malunje, ayi<br />

ndithu sindingawadziwe, mpang’ono pomwe.”<br />

“Aaa! zoonadi?”<br />

“Zoonadi pali agogo kumanda.”<br />

“Tiyeni mukawadziwa lero.”<br />

“Ndakondwanso podzandiitana ine. Koma dzuwa<br />

lisanalowe, Kansireyo akhala atachira.”<br />

“Zoonadi zimenezi?”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

239


“Eee, ine ndimanena zoona zokhazokha. Palibe<br />

ng’anga yoopsa ngati ine m’dziko lonse lino. Ndili ndi<br />

mankhwala anga owopsa kwambiri.”<br />

“Mudakatenga kuti mankhwalawo?”<br />

“Kwathu kudziko la mbewa.”<br />

“Kodi inu ndimayesa kuti kwanu ndi kwathu kudziko<br />

la mbalame. Kodi inu sindinu m’bale wathu?”<br />

“Ndine m’bale wanu.”<br />

“Nanga bwanji mukuti kwanu ndi kwa mbewa?”<br />

“Inenso ndikufunseni. Kodi inu kwanu n’kuti?”<br />

“Ndakuuzani kale kuti kwathu ndi kwa mbalame.”<br />

“Osati kwa ng’ombe?”<br />

“Chifukwa?”<br />

“Nanga inu mwadabwa ndi chiyani poti muziti ndikati<br />

kwathu ndi kwa mbewa mudodoma. Inenso ndili<br />

kudodoma poti mukuti kwanu n’kwa mbalame pomwe<br />

ine ndikuona kuti kwanu n’kwa ng’ombe.”<br />

“Chifukwa chiyani?”<br />

“Achimwene ndikuuzeni. Inu kwanu n’kuwiri: kwa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

240


ng’ombe ndiponso kwa mbalame.”<br />

“Mwaneneranji zimenezi?”<br />

“Taonani chilinundacho! Ine kwathu n’kwa mbewa ndi<br />

mbalame. Tonsefe ndife ofanana tilibe kwathu<br />

kwenikweni ayi. Izi tinazivala mosasankha ayi,<br />

tinangopezeka monga tililimu ndiponso . . . ”<br />

“Pepani sing’anga tiyeni tingakapeze maliro.”<br />

Dzidzidzi, mbaleme zonse ku makololo kuja<br />

zidangoona a Chiuzimbi ndi a Mleme ali kutera pansi<br />

koma maso a Mleme anali pa Kadzidzi gaa, chifukwa<br />

adaona kuti mutu wake unali wotupa. Mleme<br />

mumtima mwake anaganiza kuti mbalame ija<br />

yotchedwa Kansire ndi Kadzidzi uja, poona<br />

kutupikana kwa mutu.<br />

Nthawi yomweyo anatulutsa lumo lakuthwa kwambiri<br />

pamodzi ndi mankhwala ake. Posakhalitsa mbalame<br />

zonse zinaona kuti mutu wa Kadzidzi watemedwa kale<br />

magazi ali psuu, mankhwala ali kupakidwa.<br />

“Pepani sing’anga, ine sindikudwala ayi,” anatero<br />

Kadzidzi.<br />

“Kodi wodwala mutuyo sindiwe?” anafunsa Mleme.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

241


“Ayi sindine.”<br />

“Nanga ndi ndani?”<br />

“Kansire.”<br />

“Ali kuti?”<br />

“Kuchisa chake.”<br />

“Nanga iwe sukudwala?”<br />

“Ayi.”<br />

“Nanga mutuwu unatupa n’chiyani?”<br />

“Siwotupa, ndi mmene ndinabadwira basi, monga<br />

momwe mulili inumu. Mumaoneka ngati mnzathu<br />

mbalame, komanso ena amati ndinu mbewa. Kodi<br />

zikatero chikhale chifukwa choti ife tikutemereni<br />

mankhwala kuti umbewa muli nawowu ukuchokeni?”<br />

“Aaaa, . . . chipongwe choopsa, ndizo<br />

m’mandiyitanira?” anatero Mleme ali kuuluka<br />

kuthawira m’malunje, mbalame zonse zili maso yuu,<br />

kumupenya koma chimutu cha a Kadzidzi chili magazi<br />

psuu.<br />

Phunziro: Si bwino kumaweruza anthu pongotengera<br />

maonekedwe chifukwa maonekedwe amapusitsa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

242


Mafunso<br />

1. Kodi ndi mbalame iti imene inali yotchuka ndi<br />

phokoso?<br />

2. N’chifukwa chiyani mbalameyi inkaona kuti<br />

ndi bwino kuti Kansire akhale mfumu?<br />

3. Mukuganiza kuti n’chiyani chinachititsa kuti<br />

Chiuzimbi abwere mochedwa?<br />

4. Kodi Kansire sanapite kuphwando lija<br />

chifukwa chiyani?<br />

5. N’chiyani chinachititsa Mleme kuganiza kuti<br />

amadwala mutu ndi Kadzidzi?<br />

6. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

243


Chikumbumtima Chidapha Njovu<br />

Kalekalelo, Njovu inkacheza kwambiri ndi Kalulu.<br />

Tsiku lina inapita kwa Kalulu, n’kumupeza kulibe,<br />

koma inapeza panja patayanikidwa ndiwo. Itaona kuti<br />

palibe aliyense akuona, inaganiza zongoziba. Kenako<br />

Njovu inatenga ndiwozo n’kumapita nazo kwawo.<br />

Kalulu atafika n’kupeza ndiwo zake zitabedwa,<br />

anaganiza zokafunsa bwenzi lake la pamtima Njovu.<br />

Kalulu anafunsa a Njovu kuti, “A Njovu, kodi<br />

mwatenga ndiwo zanga ndinu?” A Njovu anakana kwa<br />

m’tu wagalu, amvekere, “Ndatenga si ine!” Kenako<br />

Kalulu anati, “Koma ngati mwatenga ndinuyo<br />

n’kumakana, chikumbumtima chikuphani!” Kenako<br />

Kalulu anaona msana wa njira. Njovu m’mbuyo muno<br />

inayamba kuda nkhawa kwambiri. Inkaganiza kuti<br />

chikumbumtima ndi nyama yaikulu komanso<br />

yamphamvu kwambiri kuposa iyoyo, choncho<br />

inayamba kukhala mwamantha. Inasiya kutuluka<br />

panja kukafuna chakudya poopa kukumana ndi<br />

chikumbumtima. Masiku anadutsa Njovu ikungogona<br />

nayo njala moti inaonda kwambiri. M’kupita kwa<br />

nthawi Njovu inafa. Apa mawu a Kalulu aja anathera<br />

mu siizi, Njovu inaphedwa ndi chikumbumtima.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

244


Phunziro: Ukachita chinthu choipa chikumbumtima,<br />

chomwe ndi munthu wamkati, chimakuimba mlandu<br />

moti utapanda kuvomereza kulakwa kwako ukhoza<br />

kufa ndi nkhawa.<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi chikumbumtima ndi chiyani?<br />

2. Kodi Njovu inkachidziwa chikumbumtima?<br />

3. Kodi n’chiyani chinapha Njovu?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

245


Chifukwa Chake Chule Amakhala M’madzi<br />

Pamudzi wina panali mayi ena odziwa kulikazinga<br />

thobwa. Dzina la mayiwa linali Zenje. Anzawo ena<br />

achilomwe ankangowatchula kuti mayi Nalimata.<br />

Anthu ambiri ankabwekera thobwa la mayiwa moti<br />

anthu sankatha phazi pakhomo pawo. Mwamwayi,<br />

mayi Zenje anali munthu wochereza alendo.<br />

Ankalandira aliyense amene wabwera kudzacheza<br />

ndipo ankamupatsa chipanda cha thobwa kuti<br />

azizilitse kukhosi. Sankasamala ngakhale zitakhala<br />

kuti munthuyo ndi kabwerebwere. Koma panali<br />

munthu wina wopanda pabwino, yemwe ngakhale<br />

mayiwa ankamuchitira zabwino zonsezi,<br />

ankawaberanso thobwa lawo. Munthu ameneyu dzina<br />

lake linali Chule. Ankati mayi Zenje akangochoka<br />

kupita kuchitsime kapena kumsika, iyeyo<br />

ankawalowela m’nyumba n’kuwabera thobwa. Mayi<br />

Zenje akabwera ankadabwa kuti thobwa lawo latsika.<br />

Kenako anazindikira kuti pali tambwali wina yemwe<br />

akumapungula thobwalo ndipo anatsimikiza mtima<br />

zomukhaulitsa. Kuyambira tsiku limenelo<br />

anachenjera, moti anayamba kukhoma chitseko<br />

chawo. Chulenso naye anazindikira kuti amutulukira<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

246


ndipo anapeza njira ina yobera thobwalo ngakhale<br />

zitakhala kuti pakhomo ndi pokhoma. Mayi Zenje<br />

ataona kuti kukhoma chitseko sikukuthandiza,<br />

anaganiza zowiritsa kwambiri thobwalo kuti wakubayo<br />

akabwera limuwaule. Ndiyeno anawiritsa thobwa<br />

lomwe anaphika tsikulo n’kuliika pakona la nyumba<br />

yawo. Kenako anadendekera mtsuko wawo n’kumapita<br />

kumadzi. Chule ataona kuti mphaka wachoka, anaona<br />

kuti yakwana nthawi yoti khoswe asangalale. Popeza<br />

pakhomo la nyumba ya mayi Zenje panali potseka,<br />

anapita kuseri kwa nyumbayo n’kukwera pamtondo.<br />

Kenako anasolola bango lake n’kulilowetsa mumtsuko<br />

unali pakona uja kudzera pazenera. Kenako<br />

anayamba kupopa thobwalo ndi mlomo wake. Monga<br />

mwa masiku onse, iye ankayembekezera kumva<br />

kuzuna kwa thobwalo. Koma patsikuli anakumana<br />

nazo. Thobwa lothenthalo linamulowa kukhosi moti<br />

anabuula koopsa. Thobwalo linawauliratu kukhosi<br />

kwake ndipo mawu ake anasinthiratu. Kenako<br />

analumphira pansi ndipo thobwa lija linapitirizabe<br />

kutuluka m’bango lija moti linayamba<br />

kumupungukira pamsana. Msana wonse unatuluka<br />

matuza ndipo nthawi yomweyo anathamangira<br />

kumadzi kuti akadziziziritse. Kungoyambira nthawi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

247


imeneyo, Chule anayamba kukhala m’madzi kuti<br />

asamamve kupweteka kwambiri chifukwa cha matuza<br />

anali pansana pake aja.<br />

Phunziro: Kuba ndi koipa. Kuba ndi kutenga chinthu<br />

cha mwiniwake popanda chilolezo.<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi mayi Zenje anali munthu wotani?<br />

2. Kodi anatani atazindikira kuti thobwa lawo<br />

likubedwa?<br />

3. Kodi Chule anasiya kuba thobwa ataona kuti<br />

mayi Zenje akumatseka chitseko chawo?<br />

4. Kodi mayi Zenje anatani pofuna kukhaulitsa<br />

amene ankawabera thobwa lawo?<br />

5. N’chifukwa chiyani mawu a chule anasiya<br />

kumveka bwino?<br />

6. N’chifukwa chiyani Chule amakhala ndi zilonda<br />

pamsana?<br />

7. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

248


Kufulumira Kunena Anathawitsa Likongwe<br />

wa Apongozi<br />

Panali anyamata awiri amene anakwatira banja<br />

limodzi. Wina anakwatira wamkulu wina anakwatira<br />

wamng’ono. Tsiku lina apongozi awo anadwa la<br />

matenda odetsa nkhawa. Atapita kwa sing’anga<br />

anawauza kuti mankhawala amene angathandize kuti<br />

apongoziwo achile ndi mbewa ya Likongwe. Akamwini<br />

awiri aja atamva zimenezi ndiponso pokhala odziwa<br />

kusaka ndi kukumba mbewa, analonjeza kuti apeza<br />

Likongwe amene anali kufunikayo. Tsiku lotsatira<br />

mkamwini wamkulu uja anauza mkamwini<br />

wamng’ono pamodzi ndi anzawo amene amachita<br />

nawo chidyerano kuti apite kokapha Likongwe<br />

chifukwa anali ataona pamene pamalowa Likongwe.<br />

Asanayambe kukumba, mkamwini wamkulu uja anati,<br />

“Amene athawitse Likongwe wa apongoziyu akachoka<br />

pamudzi paja.” Mkamwini wamng’ono pofuna<br />

kusonyeza ulemu kwa mkamwini wamkulu anayamba<br />

kukumba. Pasanapite nthawi, Likongwe anadziwa kuti<br />

zinthu zavuta, kenako anabulika kudzenje lija<br />

n’kulinjika mbali imene kunakhala mkamwini<br />

wamkulu uja. Mkamwini uja chifukwa chamantha<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

249


anajowa, osadziwa kuti akupereka mpata woti<br />

Likongwe athawe. Likongwe analowa patchire<br />

osaonekanso. Mankhwala othandizira apongozi<br />

sanapezeke. Tsopano ena anafunsa kuti, “Wathawitsa<br />

Likongwe ndani?” Mkamwini wamkulu anayesetsa<br />

kupepesa koma chifukwa anali atanena kale yekha<br />

kuti amene athawitse Likongweyo achoka pamudzipo,<br />

anakakamizika kuchoka ndi mkazi wake. Mkamwini<br />

wamng’ono ndi amene anapitiriza kukhala pamudzipo.<br />

Phunziro: Osamafulumira kuyankhula chifukwa<br />

umatha kudziika wekha pakona.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani akamwiniwa ankakumba<br />

Likongwe?<br />

2. Kodi mkamwini wamkulu ananena kuti amene<br />

athawitse Likongwe achita chiyani?<br />

3. Kodi zimene ananenazi zinamubweretsera<br />

mavuto otani?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

250


Mlendo Ndi Mame<br />

Kalekale panali mayi wina dzina lake Nasiketi. Nasiketi<br />

anali kudziwika kwambiri chifukwa cha umbombo.<br />

Tsiku lina anavuula mphale, ndipo atasinja ufa<br />

anaganiza kuti ndiwo zimene adyere nsima tsikulo<br />

zikhale nyama. Anasinjadi ufa wosalala bwino<br />

ndiponso anapezadi nyama yonona bwino imene<br />

anakagula pamudzi woyandikana ndi mudzi wawo. Pa<br />

nthawiyi Nasiketi anali asanataye matsukwa a mphale<br />

ija. Akumaliza kuphika nsima anamva panja munthu<br />

wina akuodira. Poonetsetsa anaona kuti ndi mlendo<br />

amene sanali kumuyembekezera. Apa nzeru<br />

zinamuthera Nasiketi. Ananyamula nsima ndi kuika<br />

pamphika wa nyama uja kenako n’kuika mphika wa<br />

nyama ndi nsima ija pakamwa pa mtsuko umene<br />

munali matsukwa uja. Tsoka ndi ilo nyama ndi nsima<br />

ija zinagwera m’matsukwa muja. Atatuluka panja kuti<br />

akumane ndi mlendo uja, mlendoyo anamuuza kuti,<br />

“Pepani ndi wosakhalitsa, ndimafuna mundigawireko<br />

madzi akumwa.” Mlendoyo atamwa madziwo<br />

ananyamuka n’kumapita.<br />

Phunziro: Umbombo kapena dyera zimawonongetsa<br />

zambiri.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

251


Mafunso<br />

1. Kodi Nasiketi anali ndi khalidwe lotani?<br />

2. Kodi ataona kuti kwabwera alendo anachita<br />

zotani kuti alendowo asadye nawo nsima yake ya<br />

ndiwo nyama?<br />

3. Kodi alendowo anabwera kunyumba kwake<br />

chifukwa chiyani?<br />

4. Kodi mukuganiza kuti Nasiketi anasangalala<br />

ndi nsima ija?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

252


Ukasauka Usamagwira Nyanga<br />

Mkulu wina anakafunsira ntchito kwa bwana<br />

wolemera kwambiri. Kumene ankagwira ntchitoko<br />

anapezako anzake amene anali atakhala kwa nthawi<br />

yaitali ndi bwanayo. Anzakewo anali ndi zinthu<br />

zambiri zimene anapata pa zaka zimene anakhala<br />

akugwira ntchito. Chifukwa chosirira kukhala ndi<br />

katundu ngati wa anzakeyo ndiponso kukhala<br />

wolemera, anaganiza zoti apeze mankhwala. Mumtima<br />

anaganiza kuti mankhwalawo amuthandiza kuti<br />

bwana wake azimukonda, kuti iye akhupuke ndiponso<br />

kuti bwanayo achotse ena mwa anzake ena amene<br />

sankagwirizana nawo. Ngati zimenezi zikanatheka<br />

ndiye kuti iye akanalandira udindo ndiponso<br />

akanamuwonjera malipiro ake. Atapita kwa sing’anga<br />

anapezadi mankhwala amene ankafunawo. Sing’anga<br />

uja popereka mankhwalawo anamuuzitsa kuti<br />

asakagone kwa masiku atatu chifukwa ngati<br />

angakagone ndiye kuti akatupa mimba. Koma tulo ndi<br />

nkhondo timagoneka olira. Tsiku loyamba analimbadi<br />

m’maso osagona. Pamene kunkacha tsiku lachiwiri<br />

tulo tinali titasonkhana, moti amati akati aimirire<br />

sizimatheka. Atakhala pansi kuyambika kwa matenda<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

253


kunali komweko. Anzake amene ankafuna kuwalodza<br />

aja atamufunsa anafokotokoza kuti, “Pepani anzanga,<br />

munthune ndimafuna kulemera. Ndiye mankhwala<br />

amene ndinapeza, chizimba chake china n’choti<br />

ndisagone masiku atatu, koma ndalephera<br />

kuchikwaniritsa. Motero thamangani mukamuuze<br />

sing’anga wandipatsa mankhwalawa kuti atsukule<br />

nyangayo n’cholinga choti ine ndikhale ndi moyo.”<br />

Anzake aja atapita anakapeza kuti sing’anga uja anali<br />

atamwalira cha dzana lake moti anthu anali<br />

asanachoke pasiwa. Anzake atabwerako<br />

anamufotokozera mmene ayendera. Chifukwa<br />

chodziwa kuti kwake kwatha anayamba kulira ndipo<br />

polirapo anali kulira mochenjeza kuti, “Abale anga<br />

munthu ukasauka si nzeru kugwira nyanga, taonani<br />

zandichitikira inezi!” Pamenepo anzakewo<br />

anavomerezadi kuti, “Ukasauka usamagwire nyanga.”<br />

Nyanga zimene munthu uja anakatenga ndi zimene<br />

zinam’phetsa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

254


Phunziro: Anthu ambiri a ku Africa kuno<br />

amakhulupirira zanyanga kapena ufiti, koma ngati<br />

atasukusula akhoza kuona kuti ufiti kulibe. Mwambi<br />

wakuti ukasauka usamagwira nyanga<br />

umangochenjeza kuti zikativuta tisamachite zinthu<br />

zomwe zingatiike m’mavuto kapena kumafunira<br />

anzathu zoipa.<br />

Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani mkuluyu anapita kwa<br />

asing’anga?<br />

2. Kodi kusakhutira ndi zomwe tili nazo<br />

kungabweretse mavuto anji?<br />

3. Kodi mwambi wakuti ukasauka usamagwira<br />

nyanga umatanthauza chiyani?<br />

4. Kodi tikuphunzira chiyani m’nkhaniyi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

255


Ulenje Umasimba Wako<br />

Kalekale panali munthu wina amene anapita kuthengo<br />

kukapha nyama. Kumeneko anapha nyama ziwiri.<br />

Pamene ankabwerera kwawo n’kuti kunja kuli<br />

kachisisira ndipo anamva phokoso likumveka m’mudzi<br />

wakwawo. Atafika pamphambano, mwadzidzidzi<br />

anangoona mkango watulukira. Mlenjeyo anachita<br />

mantha kwambiri, koma mkango uja unamuuza kuti,<br />

“Musachite mantha achimwene. Panotu takumana<br />

amuna okhaokha. Kaya inu mukuchokera kuti<br />

ulendowu?” Poyankha munthu uja anati: “Ine<br />

ndikuchokera m’malunjemu ndimakasaka.” Ndiyeno<br />

mkango unati, “Popeza tonse tikuchokera kosaka,<br />

aliyense asaulule mnzake. Ulenje umasimba wako,<br />

osati wamnzako.” Atangosiyana pamenepo, mkango<br />

uja unalowa m’tchire ndipo munthuyo anathamangira<br />

kwawo ali ndi mantha. Kenako anayamba kuuza<br />

anthu kuti wakumana ndi mkango utagwira nyama.<br />

Mkango uja utamva zimenezi, unapita kunyumba kwa<br />

amfumu n’kukagwira mwana wawo n’kumupha.<br />

Kenako unakamuika m’nyumba mwa mlenje uja.<br />

M’mudzimo munayambika chipwirikiti chifukwa cha<br />

kusowa kwa mwanayo ndipo mfumu inalamula kuti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

256


anthu afufuze amene watenga mwana wakeyo.<br />

Atafufuza anapeza mwanayo atafa koma ali m’nyumba<br />

mwa mlenje uja ndipo mfumu inalamula kuti nayenso<br />

aphedwe.<br />

Phunziro: Si bwino kumaulula zinthu zomwe iwenso<br />

wachita nawo, zimabweretsa mavuto.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi mkango unkachokera kuti nanga mlenje<br />

uja ankachokera kuti?<br />

2. N’chifukwa chiyani mkango unanena kuti<br />

ulenje umasimba wako?<br />

3. Kodi mlenjeyo analakwitsa chiyani?<br />

4. Nanga anakumana ndi mavuto otani?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

257


Angozo ndi Mwana Wawo<br />

Bambo: Iwe Joni, kodi pulezidenti woyamba m’Malawi<br />

muno anali ndani?<br />

Mwana: Joyce Banda.<br />

Bambo: (Phwaaa! anamuswa khofi) Uzikhala siliyasi<br />

ndi maphunziro ako!<br />

Mwana: Oo! pepani, ndimaona ngati mumafunsa<br />

pulezidenti woyamba wachizimayi.<br />

Bambo: Khala chete chimwana chopanda nzeru iwee!<br />

Ngati zikukuvutani zakupulaimale, ndiye<br />

zakusekondale mukaphula kanthu inu?<br />

Mwana: Chabwino, nanga inu bambo, Abengo ndi<br />

ndani?<br />

Bambo: Mlimi wa fodya.<br />

Mwana: (Phwaaa! naye analipulumutsa lake khofi)<br />

Abengo ndi chibwenzi cha amayi! Muzikhala siliyasi<br />

ndi banja lanu inu!<br />

Bambo: Mwanawe ndiuze zambiri.<br />

Mwana: Khalani chete. Ngati mukulephera kudziwa za<br />

akazanu musanakalambe, nanga mukadzakalamba<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

258


ndiye zidzakhala bwanji?<br />

Phunziro: Aliyense amachita bwino mbali inayake.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi n’chifukwa chiyani Angozo anamenya<br />

mwana wawo?<br />

2. Kodi makambitsirano a bambo ndi mwanayu<br />

akusonyeza bwanji kuti onse anali ndi nzeru?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

259


Ufulu wa Nkhwere<br />

Tsiku lina Nkhwere zinachoka m’nkhalango n’kufika<br />

pakhonde la sukulu yotchedwa Nfunde. Mtsogoleri wa<br />

Nkhwere anali Goloti. Goloti anasuzumira pawindo<br />

n’kuona mnyamata wina dzina lake Sibo akusewera<br />

m’kalasi ndipo anamuuza kuti: “Iwe Sibo, ife timafuna<br />

kuimba nawo sukulu, kodi aphunzitsi ako ali kuti?”<br />

Sibo anati, “Ine ndinatsiriza kale, tsopano ndine<br />

mphunzitsi.” Koma Goloti anati, “Kodi sudziwa kuti<br />

iwe ndi ife ndi mtundu umodzi? Inuyo munachokera<br />

kwa ife, mumangoona kunyada inuyo. Inu anzathu<br />

mumavala malaya ndi kabudula, ife timangokhala<br />

osavala, kodi mulibe manyazi kumanyoza ife makolo<br />

anu? Pakanapanda ife mukanaoneka inu?” Koma Sibo<br />

anati, “Sindikukudziwani ayi! Inu ndi anyani a<br />

m’tchire!” Koma Goloti anati, “Eee! Mwana uyu<br />

n’ngosaphunzira. Kawerengenso mabuku ako. Ife<br />

tsopano tikufuna ufulu womaimba sukulu pamodzi<br />

ndi inu, ndiponso tizichita zibwenzi ngakhalenso<br />

kukwatirana.”<br />

Sibo: “Chokani anyani inu!”<br />

Goloti: “Eee! Mwana iwe ukuchitira chipongwe makolo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

260


ako, ndithu mukapitiriza kuchita mwano umenewu<br />

mvula simuiona chaka chino.”<br />

Sibo: “Chokani inu! Chokani!”<br />

Goloti: “Ine ndi wapampando wa anzangawa.<br />

Tapangana m’tchire m’dalaka njoka. Ife tonse tikufuna<br />

tibwerere kumudzi kuno, tizidyera pamodzi, ndiponso<br />

tizimwera pamodzi.”<br />

Sibo: “Pakati pa ife ndi inu ayi, chibwenzi<br />

sichingakhalepo. Inu adakusankhirani Fulu kuti<br />

muchite naye ubwenzi.”<br />

Goloti: “Chabwino, tsala bwino, ife tipita kwa Fuluyo.<br />

Koma kawerengenso mabuku. Iwe unachokera mwa<br />

ife. Onani kamwana kosaphunzira, kawerenge<br />

mabuku a Dalawini, akakuuza. Onani umbuli! Funsa<br />

aphunzitsi ako!”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

261


Mafunso:<br />

1. N’chifukwa chiyani nkhwere zinkanena kuti ndi<br />

pachibale ndi Sibo?<br />

2. Kodi munthu ndi nyani ndi zofananadi?<br />

3. Kodi mukuganiza kuti nkhwere italowa<br />

m’kalasi n’kukhala padesiki ingaphunzire<br />

kalikonse?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

262


Ubwenzi wa Nkhumba ndi Nkhosa<br />

Kalekalelo, pakati pa Nkhosa ndi Nkhumba panali<br />

chibwenzi chonyambitana mapazi. Kumene Nkhosa<br />

inkayenda, Nkhumba inkakhala komweko. Anthu onse<br />

ankasilira chibwenzi chosaonekaoneka chotere. Kalulu<br />

nthawi zonse amati akamva za chikondi chotere<br />

sankamva bwino, kumtima kwake kunali nsanje.<br />

Tsiku lina Kalulu ankakambirana ndi mkazi wake<br />

amvekere, “Kodi iwe wamva za chikondi cha Nkhosa<br />

ndi Nkhumba?” Poyankha mkazi wake anati, “Eee!<br />

Anzanutu amenewo. Si zainuzi. M’nyumba<br />

kumangokangana tsiku ndi tsiku. Ndiponso pakhomo<br />

panga pano, ndimangokhalira kulandira milandu.<br />

Kumene mumayendako ntchito ndi bodza komanso<br />

kuchenjeretsa anthu. Mbiri ili buuu! Akuti<br />

kuchenjera! Banja lanunso likukukanikani kusamala!”<br />

Kalulu atamva mawu amenewa anati, “Izo udamvazo<br />

ndi za nsanje. Anthu amachita nsanje ndi ine popeza<br />

ife a Kalulu ndife amuna osati masewera. Mfumu<br />

yamuno m’nkhalango yomveka ngati kulira kwa<br />

mphenzi nthawi ya mvula.”<br />

Tsopano kalulu analowedwa mzimu woyipa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

263


Ananyamuka nalo liwiro kupita kwa Nkhumba ndipo<br />

anangoti balamanthu! nati, “Moni a Nkhumba! He-e-e!<br />

ati ndili ndi bwenzi! Mwamva kodi?” Kenako a<br />

nkhumba anati, “Zotani? Za bwenzi zotani?” Kalulu<br />

anati, “Suja akuti bwenzi lanu ndi a Nkhosa? Ine<br />

ndathamanga kudzaulula zimene anandiuza.” “Ine<br />

sindifuna kumva chilichonse chokhudza bwenzi langa<br />

Nkhosa, bwenzi lapamtima,” anatero a Nkhumba.<br />

Kenako Kalulu anati, “A Nkhosa amakunenani ati inu<br />

ndinu auve wodya zotoleza m’matope, ati ndinu<br />

msambamatope.”<br />

Tsopano nkhumba inautsa mutu wake kuti imve<br />

zonse.<br />

Kalulu: “Tere amatinso inu ndinu wamatekenya.”<br />

Nkhumba: “Tsopano ndakhulupirira, iwe Kalulu ndiwe<br />

wabwino. Iweyo ukhala bwenzi langa. Uzindiuza zonse<br />

zimene Nkhosa izinena.”<br />

Kalulu: “Chabwino ndavomera chibwenzi chapakati pa<br />

inu ndi ine.”<br />

Nkhumba: “Tsopano pita bwino bwenzi langa. Koma<br />

wosakamuuza Nkhosa kuti ndapanga ulendo<br />

wokamuphwasura iyeyo.”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

264


Kalulu analiyatsa liwiro lopita kwa Nkhosa. Atayipeza<br />

Nkhosa anati:<br />

Kalulu: “O! o! Kodi mulipo? Akadakhala kuti amafa<br />

ndi mjedo, kunena zoona n’kadakupezani mutafa.”<br />

Nkhosa: “Kwagwa chiyani?”<br />

Kalulu: “Ee ho! Ine panjira ndinakumana ndi a<br />

Nkhumba, zimene amanena zosonyeza kuti zija<br />

timamva kuti mumakondana, n’zabodza.”<br />

Nkhosa: “Amati chiyani iyeyo?”<br />

Kalulu: “Amati inu ndinu wanyansi ati sadzadyera<br />

nanu pamodzi popeza muli ndi matenda a mamina<br />

wosatha, amangochucha ngati mtsinje. Msipu wonse<br />

ati inu mudagwetsera mamina mudawononga.”<br />

Nkhosa: “Amatero iyeyo?”<br />

Kalulu: “Iwowo ndithu ndiwo amatero.”<br />

Nkhosa: “Kuyambira lero chibwenzi chachipongwe<br />

chotere chatha. Tsopano iweyo ndiwe bwenzi langa<br />

chifukwa umanena zoona, ndipo ndili pa ulendo<br />

kupita kwa iyeyo kuti ndikamuphulitse.”<br />

Pamene nkhumba inatsiriza kukwera chitunda<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

265


chopitira kwa Nkhosa inangoti, gululu yakumana ndi<br />

Nkhumba. Eee, panalitu moto!<br />

Nkhumba: “Bwanji iwe umandinena, lero kuli<br />

ndikupha!”<br />

Nkhosa: “Iwenso umandinena, ndamva kwa kalulu<br />

bwenzi langa. Lero ndikufinya.”<br />

Kupandana kwa awiriwa kunamveka ponseponse<br />

ndipo chibwenzi chinatha. Kalulu anati kwa mkazi<br />

wake: “Suja unkanena kuti chikondi chikundikanika,<br />

n’kumayamikira a Nkhumba ndi a Nkhosa, wamva<br />

tsopano zimene zachitikazi? Heede!<br />

Ndimangokumvetserani!”<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi mkazi wa Kalulu ankadandaula chiyani?<br />

2. Kodi khalidwe la Kalulu linali lotani?<br />

3. N’chifukwa chiyani Nkhosa ndi Nkhumba<br />

zinapandana?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

266


Mvundula Madzi<br />

Kalekalelo panali midzi iwiri imene anthu ankamvana.<br />

Anthu ambiri anali kusirira machitidwe a midziyi.<br />

Mayina a midzi anali Mchirawagaru, mwachidule<br />

amati mudzi wa Mchira. Winawo unali mudzi wa a<br />

Zeze.<br />

Pakati pa mudzi wa Mchira ndi wa Zeze, panali<br />

chitsime chotchedwa Namtudza. Chitsimechi chinali<br />

chokumba ndipo chinazunguliridwa ndi mitengo ya<br />

nkhadze cha kumtunda kwake. Kumunsi kwake<br />

kunali mtengo wamango ndipo chakumwera kwake<br />

kunali mtsinje umene udagwera ku Mtema, ku<br />

Phukuto m’mudzi mwa a Mchira modzera kumalo<br />

wotchedwa Danani, mpaka m’chikonde pafupi ndi<br />

Nzama kukaphera mumtsinje wa Namachizi. Kunsi<br />

kwake kunali dziwe lotchedwa Kanyinda.<br />

Chimbalame chotchedwa Mvundulamadzi,<br />

mwachidule amati Vundula chinali kumwera pa<br />

chitsime cha Namtuza, chimwera ku Mtema,<br />

Chimwera pa Chimkonde, mpaka dziwe la Kanyinda.<br />

Mbalameyi inali kuuluka pamwamba pa midzi iwiriyi,<br />

Mchira ndi Zeze, ndipo chifukwa cha kumvana kwa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

267


midzi iwiriyi Vundula sankakondwera ayi. Popeza<br />

Mbalame zotere zimakondwera zikaona chidani,<br />

maliro, ndewu kapena kuzokozana.<br />

Tsiku lina chinagona mumtengo wamkuyu pa<br />

Kanyinda. Mmawa chinalawira kuchitsime cha<br />

Namtunda ndipo chinaona gulu la akazi lasenza<br />

mitsuko kukatunga madzi. Gululi linali la kwa<br />

Mchirawagalu. Atatha kutunga, chimbalamechi<br />

chinalowa pachitsime paja basi n’kudetseratu madzi<br />

aja chimvekere, vu! vu! vu! Ndi mapiko ake aja, phi<br />

phi! phi! Madzi onse kuderatu kuti bii!<br />

Chitatero chingangoti vuuku, bisalu mumtengo wa<br />

Nkhadze. Tsopano akazi a kwa Zeze analipo khumi.<br />

Atafika pachitsime anapeza madzi ali bii! Mtsikana<br />

wina wotchedwa Maleyi anati, “Oo anzathu onani<br />

madzi ada! Komatu akazi a kwa Mchirawagaru atunga<br />

pompano. Basi iwowo ndi amene adetsa madzi.<br />

Akufuna kuti chitsime chikhale chawo chokha.<br />

Tsopano tadziwa, a Mfumu a Mchira akudana ndi a<br />

Zeze, awatuma ndi amfumu kuti adzachite zimenezi!”<br />

Akazi onse anabwerera osatunga madzi mpaka ena<br />

anapita kukatunga kuchitsime cha Namachizi.<br />

Chimbalame chija chitaona zimenezi chinangoti,<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

268


“Ehede! Basi zakhala bwino. Tsopano cholinga changa<br />

chakwaniritsidwa.”<br />

Tsiku lina m’mawa chimbalame chija chinasokoloka<br />

m’nthochi za m’madimba a ku Dumbzi, kulawirira ku<br />

Namtunda kukadetsanso madzi akazi a kwa a Zeze<br />

atatunga kale. Pobwera a kwa Mchira anapeza madzi<br />

akuda. Mtsikana wina dzina lake Damalesi anati,<br />

“Onani akazi a kwa Zeze adetsa madzi, awapangira ndi<br />

amfumu awo.” Onse anabwerera ndipo Mbalame ija<br />

pakumva inati, “Eheee, zanga zikuyenda bwino.”<br />

Potsiriza, midzi yonse inadodoma popeza mfumu<br />

ziwirizi zinafunsana pabwalo. Tsopano a Zeze ndi a<br />

Mchira anapangana kukakhalira ku chitsime kuja ndi<br />

nduna zawo. Mmawa kukucha, anaona chimbalame<br />

chabwera m’madzi muja lowu, chimvekere mapiko<br />

tambasulu, chayamba kuvu! kuvu! kuvu!<br />

Onse aja anathamanga ndi uta, basi n’kuchilasa ndipo<br />

chinafera pomwepo. Zitamveka izi, a Zeze ndi a<br />

Mchirawagaru pamodzi ndi anthu awo, anayanjananso<br />

chifukwa anapha mvundula madzi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

269


Phunziro: Ifenso tiziyamba tapha mvundulamadzi<br />

tisanayambe kudana.<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi mbalame yotchedwa Vundula<br />

inkasangalala pakachitika zotani?<br />

2. N’chifukwa chiyani midzi ya a Mchira ndi a<br />

Zeze inadana.<br />

3. Kodi anatani kuti adziwe amene ankadetsa<br />

madzi?<br />

4. Nanga ifeyo tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

270


Chifukwa Chake Ng’ona Imakhala M’madzi<br />

Kalekale dzikoli likali nsoka, panali mfumu ina<br />

yomveka kwambiri m’dziko lotchedwa Peta. Dzina la<br />

Mfumuyi linali Chifuyo.<br />

Dziko la Peta lidali loopsa. Kudali nkhalango ndipo<br />

m’nkhalangoyo mudali zilombo zosiyanasiyana zoopsa,<br />

kuyambira zokwawa mpaka zoyenda. Zimamveka kuti<br />

kunali njoka zowuluka ngati mbalame zomwe<br />

zinkatchedwa Njokambala. Zimamvekanso kuti kunali<br />

mikango yamapiko imene inkatchedwa Mkangombala.<br />

Mfumu chifuyo inali yolimba mtima pogonjetsa<br />

zilombo zonse m’dziko la Peta. Tsiku lina, mfumuyi<br />

inaitanitsa zamoyo zonse zam’tchire. Zitasonkhana<br />

padambo, Mfumu Chifuyo inati, “Ndakondwa kuti a<br />

Njovu, a Mkango, a Njati, a Nyamalikiti kaya a<br />

Kadyansonga, a Mvuwu komanso a Kalulu afika.”<br />

Nthawi imeneyi nyama zonse zinkangopenyetsana<br />

kwinaku zikumangonong’ona. Njovu inati, “Anzathu,<br />

inu a Mkango tasenderani kuno, uzaninso a Njati<br />

akhale pafupi. Kodi a Mvuwu, munthu ameneyu<br />

atisunga muno? Onani chili m’dzanja mwakecho. Kodi<br />

sichija amatiphera nachochi?” Kodi mphamvu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

271


imeneyi, adakayitenga kuti?” A Mkango anati, “Tiyeni<br />

tileke kuyankhula, angaganize kuti tamugalukira.”<br />

Mfumu Chifuyo inati, “Tsiku lina nyama ina inabwera<br />

kudzafunsa mmene ndizikusungirani, ndiye lero<br />

ndaganiza zoti ndiyankhe nkhani imeneyi. Ndikufuna<br />

kukhazikitsa malamulo oti aliyense aziyendera.<br />

Malamulo ake ndi awa: Nyama iliyonse iziyenda<br />

mmene ikufunira. Nyama ya ndewu sikufunika.<br />

Nthawi iliyonse mukhoza kubwera kwa ine<br />

kudzadandaula. Anthu anga sadzapha ngakhale<br />

mmodzi wa inu moti akafuna nyama azipha ziweto za<br />

m’mudzi osati inu ayi.”<br />

Mkango: “Pepani mfumu tikuduleni pakamwa, ine ndi<br />

anzangawa takondwa kwambiri ndi zimene<br />

mwanenazi. Ine ndilape pamaso panu lero. Ngati<br />

mumaona anthu ena akujiwa, kudyedwa, mtsogoleri<br />

wake adali ine. Kuyambira lero, taleka chifukwa taona<br />

mtima wanu wamlerakhungwa.”<br />

Kalulu: “Tonsefe tiyeni pamodzi tikondwere tipereke<br />

kwa Mfumu Chifuyo, Hepu! Hepu!”<br />

Nyama zonse: “Huree! Hureeeeeeeee!”<br />

Tsopano msonkhano utatha nyama zidakondwera<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

272


koposa poona kuti ufumu wa Chifuyo udaposa<br />

maufumu akale monga ufumu wa a Mkango<br />

womangokudya nawo anzawo, komanso ufumu wa a<br />

Njovu womangopondereza anzawo monga a Kasenye<br />

ndi a Chule.<br />

Nyama zonse ngakhalenso Njokambala ndi<br />

Mkangombala palali kuvomera kuti Mfumu Chifuyo<br />

adzafere m’manja mwawo.<br />

Mfumu Chifuyo tsopano idaganiza zoika nduna zake.<br />

A Njovu ndi amene anasankhidwa kukhala nduna<br />

yaikulu pakati pa nduna zonse. M’nkhalango mudali<br />

chiphokoso cha chikondwerero cha zimene Mfumu<br />

Chifuyo inachita. Tsopano Njovu inasamuka kuchoka<br />

kunkhalango n’kumakhala kwa Mfumu Chifuyo kuti<br />

ikayambe udindo watsopanowo.<br />

Mwadzidzidzi, padamveka kuti Mfumu Chifuyo idapita<br />

koyendera dziko lake ndipo adakumana ndi<br />

Mkangombala ndi Njokambala ndipo zilombozi<br />

zidayamba nkhondo ndi Mfumu Chifuyo. Mwatsoka<br />

Mfumu Chifuyo sinatenge zida za nkhondo ndye<br />

idalumidwa koopsa. A Njovu atamva zimenezi<br />

anathamanga nakanyamula Mfumu Chifuyo pamsana<br />

pawo kupita nawo kunyumba. Kenako a Njovu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

273


anaitanitsa msonkhano wa nyama zonse:<br />

“Ndakuitanani ndine. Onani Mfumu Chifuyo ili gonee.<br />

Ndiyesa mwamva zimene Njokambala ndi<br />

Mkangombala achita. Mfumu ngati iyi sitidzaionanso.<br />

Taonani ine mpando umene adapatsa ife nyama za<br />

m’tchire! Tidali yani kale ife? Siuja tinkangophedwa?”<br />

Nyama zonse zinali ndi chisoni, nthawi imeneyi n’kuti<br />

Njokambala ndi Mkangombala atanjatidwa kale ali<br />

m’ndende ndiponso mapiko awo atadulidwa kale ndi<br />

asilikali. Panamveka mawu akuti Nduna Njovu<br />

ikufunidwa ndi Mfumu yodwalayo.<br />

Mfumuyo inati, “Iwe Nduna Njovu waona chipongwe<br />

chimene wachita Njokambala ndi Mkangombala. Ine<br />

ndidzayesa kubweretsa mtendere pakati pa anthu ndi<br />

nyama, koma mtendere udzavuta mpaka m’tsogolo.<br />

Kumbukirani udani wa munthu ndi njoka kuyambira<br />

pachiyambi. Ine ndimafuna kukonza chidani chimene<br />

chija, koma ndaona chimene adanena Chauta palibe<br />

munthu akhoza kusintha. Ine ndikafa, iwe monga<br />

nduna yaikulu, udzasankha yani kuti adzalowe ufumu<br />

wanga?” Nthawi yomweyo Mfumu Chifuyo inamwalira<br />

koma mawu amene idasiya anali akuti, Ufumu<br />

umenewu adzatenge ndi Mlenje monga mmene Mfumu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

274


inalili. Njovu sinali Mlenje ndipo inadziwiratu kuti<br />

Ufumu wa Chifuyo sadzalowa ngakhale anali nduna<br />

yaikulu. Koma anawuza anthu kuti alenje onse<br />

akufunika ndipo nyama zonse zisonkhane zidzamve<br />

mawu.<br />

Nyama zonse zinatchera makutu kuti zimve mawu a<br />

Nduna Yaikulu. “Zachisoni, Mfumu yathu imene<br />

timaikonda yapita kumanda kosabwerako. Onani<br />

mpando uwu wachifumu, lero ulibe mfumu yake.<br />

Pomwalira mfumu inandiuza kuti, mfumu yotenga<br />

mpando umenewu ikhale imene ili katswiri pa ulenje.<br />

Nonsenu mukudziwa kuti ine ngakhale kuti ndine<br />

Nduna Yaikulu, sindine mlenje. N’kadakhala wokonda<br />

ufumu sindikadakuuzani za mawu amenewa ayi.<br />

N’kadangokuuzani kuti kuyambira lero ndine Mfumu<br />

Chifuyo. Koma ndikufuna alenje abwere apa!” Nyama<br />

zonse zinakuwa, “Koma Njati! Ayi koma Kalulu, ayi<br />

koma N’gonaa!” “Chabwino onse abwere kuno,” idatero<br />

Njovu.<br />

Tsiku lina Nduna Njovu inasonkhanitsa nyama zonse<br />

mmawa ndipo inati, “Sindikufuna kupereka ufumu<br />

kwa bwenzi langa ayi! Koma amene angaonetse kuti<br />

ndi mlenje, alandira ufumuwu! Paja mukudziwa kuti<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

275


pali opikisana atatu: Ng’ona, Njati ndi Kalulu. Mmodzi<br />

wa atatuwa adzakhala mfumu ya tonsefe. Ndiye<br />

kudamboku kwapezeka nyama ziwiri zakufa. Kodi ndi<br />

ndani wasodza chotereyu?” Posachedwa padamveka<br />

mawu, “Ndine Bwana!” Adafulumira kuyankha Ng’ona.<br />

Onse aja, adaomba mmanja, kulemekeza Ng’ona,<br />

ndipo ena amayankhula chonong’ona kuti, “He!<br />

Komatu zadziwikiratu kuti ufumu umenewu autenga<br />

ndi Ng’ona! Chifukwa liwiro lamumchenga lifunika<br />

kuyambira pamodzi. Ng’ona ndiye wapita kale<br />

m’tsogolo!”<br />

Zimenezi Kalulu zidamuwawa mtima chifukwa ena<br />

adayamba kunyoza Kalulu, “Iwe timakukonda,<br />

ndiponso ndiwe wochenjera. Koma lero wangokhala<br />

chitsiru chenicheni, kuchenjera kuja n’kwabodza!<br />

Monga zikhale zoona kuti a Ng’ona n’kutenga ufumu<br />

iwe ulipo?” Adatero a Mbidzi.<br />

Usiku Kalulu adapita kukasaka nyama. Mwamwayi<br />

adapha Ntchefu zitatu nabwera nazo m’mudzi muja<br />

naika pakhomo pa a Njovu. Kenako iye anapita<br />

kukagona, koma popita anadzera kunyumba ya<br />

Mbidzi. “Odi! Odiii!” Kalulu adawodira. “Ndiwe ndani<br />

usiku ngati unooo?” Mbidzi inafunsa. “Ndine Kalulu!<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

276


Paja unanena chipongwe, ndapha Ntchefu zitatu,<br />

ndaika kale kwa a Njovu!” Anatero Kalulu. “Wachita<br />

bwino, ka Ng’ona kodi kapose iwe? Ife tikufuna kuti<br />

ufumu uja ukhale wako! Wachita bwino, tionana<br />

mawa.” Anatero Mbidzi.<br />

Mmawa kutacha, Njovu inakusa onse kuti abwere<br />

kunyumba kwake ndipo inafunsa kuti, “Kodi wampha<br />

Ntchefu izi ndi ndani?” Nthawi yomweyo Ng’ona<br />

inaimirira n’kunena kuti, “Ndine Bwana!” Nthawi<br />

imeneyi Kalulu anachedwa kubwera ndipo anadzapeza<br />

anthu akutamanda Ng’ona akuti, “Ayi, inu Bambo<br />

Ng’ona zanu zili kuyenda bwino, ufumuwu wadziwika<br />

kale kuti ndi wanu.” Kalulu adapita kwa Njovu<br />

n’kunena kuti, “Kodi mwaona Ntchefu zimene ndapha<br />

ine usiku?” Njovu inati, “Choka iwee! Kodi ndiwe<br />

munthu wansanje chotere?”<br />

Kalulu adamva Mbidzi ikumufunsa kuti, “Achimwene,<br />

kodi lija mumandiuza madzuloli lidali bodza?<br />

Kuchedwaku ndi manyazi kuti tingakusekeni! Anzanu<br />

a Ng’ona basi akhala mfumu yathu, kwangotsala kuti<br />

awaveke chigwinjiri kaya ndi khoza la mnyanga.”<br />

Posakhalitsa panamveka kuti pali mphekesera yoti<br />

Mfumu Chifuyo sidaphedwe ndi Njokalamba kayanso<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

277


Mkangombala, koma idaphedwa ndi anthu a m’mudzi<br />

momwemo ndiye adapanga bodza kuti aziti, Mfumu<br />

Chifuyo idaphedwa ndi zilombo. Chotero Kalulu ndi<br />

nyama zina zidatenga thupi la Mfumu Chifuyo<br />

n’kukayika pakhomo pa Njovu, naliphimba ndi<br />

masamba. Mmawa kutacha, Njovu inaitanitsanso onse<br />

kuti abwere ndipo inafunsa kuti, “Kodi pakati panupa,<br />

ndiyesa mwadziwa kuti madzulo ano tili kuponya<br />

ufumu wa Chifuyo. Iyi ndi nyama yomaliza<br />

kutsimikiza kuti wotereyu ndi mlenje wofunika<br />

kumuveka makoza awiri awa!”<br />

Anthu onse ndi nyama zonse zinayamba kukuwa,<br />

“Ng’ona! Ng’ona! Ng’ona! Ng’oooooooooooooonaaa!”<br />

Kenako njovu inati, “Mvetserani kaye. Kodi wapha<br />

imeneyi ndi ndani?” “Ndinee! Ndine Bwana!” Inatero<br />

Ng’ona.<br />

Ndiyeno Njovu inati, “Tsopano paja ena<br />

akumasokoneza, kodi alipo wina wotsutsa kuti<br />

nyamayi sadaphe ndi Ng’ona? . . . Eya, zayenda bwino<br />

lero palibe mkangano. Madzulo ano nonse mubwere<br />

kuti tidzalonge Mfumu yathu yatsopano a Ng’ona!”<br />

“Ooooooooooooooo!” Phokoso lachikondwerero<br />

linamveka. Ng’ona inati, “Lero lomwe lino potsiriza<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

278


phwando, iwe Njovu ukhala nduna yanga yaikulu!”<br />

Wagwira ntchito yako bwino!<br />

Pamene Njovu inachotsa masamba aja anali<br />

pamwamba pa nyamawa, nyama zonse zidati, “O! O!<br />

O! Onani zoopsa! Kodi udapha Mfumu Chifuyo ndiwe<br />

Ng’ona?” Ng’ona imvekere, “Hii! Ndikufa!” Waliwutsa<br />

liwiro kuthawira kumadzi, nangoti pamadzi dyuli!<br />

Mumtima mwake inati, “Koma sindidziwa, zimenezi<br />

zachitika bwanji?” Kuyambira pamenepo Ng’ona<br />

inayamba kukhala m’madzi mpaka lero.<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi nduna yaikulu ya mfumu Chifuyo inali<br />

ndani?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti Ng’ona inkaphadi nyama<br />

zija?<br />

3. Nanga anzake anatani pofuna kuikhaulitsa?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

279


Mfumu Yomveka Tambala<br />

Kale Tambala anali mfumu yomveka pakati pa<br />

mbalame zonse, ngakhalenso nyama zakutchire.<br />

Palibe wina amachita mwano kapena kusewera ndi<br />

Tambala. Onse ankamuopa popeza panali mbiri yoti<br />

ali ndi moto pamutu pake ndipo wochita naye<br />

masewera akhoza kutenthedwa. Mbiri imati onse<br />

okhudzidwa ndi motowo, basi imfa imakhala yomweyo<br />

mpaka kupserera. Motowo unali wosenzera pamutu.<br />

Ndiponso amati m’mawa kukacha Tambala<br />

ankatsokomola ndipo nthunzi wa motowo inkaonekera<br />

uli katukatu!<br />

Tambala amati akangoti, “Kokolirikooooo<br />

kwaachaaaa!” aliyense ankadzuka. Akadzatinso,<br />

“Kokolirikooo kwaachaaaaa!” aliyense ankayenera<br />

kuyamba ntchito kuopa kuti akachedwa<br />

angadzam’tenthe ndi moto uja woyaka lawilawi<br />

pamutu pake.<br />

Nyama zonse, ndi Mkango womwe, mbalame zonse<br />

mpaka Kalize kapena Ndakulapsa, zonse zinkaopa<br />

Tambala. Mbalame zinanso monga Ngolomi,<br />

Chiwombankhanga, Nthiwatiwa, Kadzidzi, Katawa ndi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

280


zina zinkaopanso Tambala. Ndiponso nyama monga<br />

Njovu, Mvuwu, Njati komanso zina zotero, nazonso<br />

zinkaopanso Tambala.<br />

Mbiri inamveka kuti wina atawupala moto wa pamutu<br />

pa Tambala, motowo sungazime mpaka wopalayo<br />

atamwalira. Anatinso sufunika nkhuni koma<br />

umangoyaka nthawi zonse. Mvula ikamagwa,<br />

ankanenanso kuti suzima ndipo umafanana ndi moto<br />

wa mphenzi woyaka mvula ili pooo!<br />

Tambala akangolira nyama zonse zimautsa ana awo,<br />

“Ana inu, ukani mfumu Tambala akuti amatumiza<br />

moto wake monga wa mphenzi kwa waulesi ndi<br />

wosamvera iye. Ukani konzekani ndithu<br />

mungatitenthetse.”<br />

Tsiku lina nyama zonse zinasonkhana pamodzi.<br />

Kalulu anati, “Anzathu, moto wa Tambalawu<br />

watiwopsa. Kumbukirani mdani wa moto ndi madzi,<br />

tiyeni kwa a Mvuwu wokhala m’madzi tikafunsire<br />

nzeru.” Atafika Kalulu anati, “Moni a Mvuwu, tabwera<br />

kuti mutipatse nzeru za moto wa Tambala. Kodi<br />

tingakaupale bwanji?” A Mvuwu anati, “Ifenso m’madzi<br />

muno tathedwa nzeru mbale wanga! Bwanji<br />

osapempha a Njovuwo kuti akapale?” Koma poyankha<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

281


a Njovu anati, “Eee! Ndaniyo, ine n’kadawukonda<br />

moyo, phukusi la moyo sakusungira ndi wina! Bwanji<br />

apite ndi a Nyamalikitiwa?” Koma a Nyamalikiti<br />

poyankha anati, “Ine ndiye toto, kodi mphenzi<br />

pakugwa mumaiwonerera? Hee! Pamakhala zoopsa.<br />

Tonsefe pano n’kutheratu psiti! Moto umene uja akuti<br />

ufanana ndi mphenzi.” Nthiwatiwa anati, “Uja ndi<br />

mdzukulu wanga. Ndipitako ndine. Moto wowopsawo<br />

ndikauwupala.” Nyama zonse zitamva mawuwa zinati,<br />

“Ooo! Wolimba mtima a nthiwatiwaaa!”<br />

Mmawa mwake, Nthiwatiwa inanyamuka ulendo<br />

kupita kwa Mfumu Tambala. Mkazi wake anasenza<br />

chipanda cha mowa. Onse anafika pakhomo pa<br />

mfumu Tambala.<br />

Atafika, Nthiwatiwa inati:<br />

Nthiwatiwa: “Zikomo Mfumu Tambala!”<br />

Tambala: “Eee! Lowani m’nyumba muno. Koma<br />

m’nyumba muno lero sadasesemo, akazi anuwa<br />

analawirira kumunda. Khalani pa chikumbapo.”<br />

Nthiwatiwa: “Ndati ndikawone mdzukulu wanga<br />

mfumu.”<br />

Tambala: “Aa! msatero mfumu sikhalapo popanda<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

282


woibereka. Mwachita bwinoo.”<br />

Nthiwatiwa: “Agogo anuwa anakutengerani<br />

kachiphera dzuwa kuti muyese kufewetsa kukhosi.”<br />

Tambala: “Ha! Mwachita bwino agogo, nanga sindiko<br />

kukhala ukuu!”<br />

Tsopano onse anayamba kumwa. Tambala anamwa<br />

kwambiri mpaka anakhuta, nagona tulo pakama<br />

wake. Nthiwatiwa inatenga ndowe yang’ombe naika<br />

pamutu wa Tambala kuti ikolere moto woopsa uja.<br />

Pamene anawona kuti ndowe sikukolera moto,<br />

anayesa kuyikapo udzu, koma zonse zinangoti zii<br />

opanda moto. Tsopano anaika nthenga zake ndipo<br />

anaona kuti sizinapse. Nthiwatiwa inauza mkazi wake<br />

kuti, “Mkazi wanga, wadziwonera wekha, timangowopa<br />

njokaluzi.”<br />

Atabwerera kwawo, anasonkhanitsa nyama zonse ndi<br />

mbalame zomwe, ndipo anati, “Ine ndinapita kuja<br />

munandituma, mboni ndi mkaziyu. Osamaopanso<br />

amene uja. Simoto uli pamutu uja, ndi litcholotcholo<br />

chabe, lidangofiira koma lilibe moto lili zii kuzizira. Ine<br />

ndidalikhudza ndi nthenga zangazi, osapsa.<br />

Ndinayikapo ndowe ya ng’ombe, mpaka udzu, ayi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

283


ndithu osapsa.” Nyama zonse zitamva izi zinati, “Ooo!<br />

Basi mfumu ndiwe!”<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi nyama zinkaopa Tambala chifukwa<br />

chiyani?<br />

2. Kodi nyamazi zinkaona kuti litcholotcholo la<br />

Tambala ndi chiyani?<br />

3. Kodi Tambala ankadzutsa athu pogwiritsa<br />

ntchito lipenga lomveka bwanji?<br />

4. N’chifukwa chiyani Nthiwatiwa inanena kuti<br />

ankaopa njokaluzi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

284


Chifukwa Chake Kadzidzi Amayenda Usiku<br />

Kalekale ku Chitimbe kumene kunali tchire la bango<br />

lokhalokha, Kadzidzi anali mfumu yoopsa. Mbalame<br />

zonse zinkagwadira iyeyo. Tsiku lina Kadzidzi<br />

anaitanitsa msonkhano.<br />

Pamsonkhanowo Kadzidzi anati, “Zikomo kuti<br />

mwabwera mwaunyinji chonchi, ine ndakhala nanu<br />

zaka zambiri muno m’Chitimbe. Palibe wina<br />

amadandaula. Ndamva kuti Mleme komanso<br />

Nthiwatiwa sakufuna kubwera. Ine monga mukudziwa<br />

ndine mfumu, tsopano ndikufuna banja lililonse<br />

lindipatse thumba la chimanga popeza malipiro anga a<br />

ufumu ndi omwewa.” Mbalame zonse zinati, “Zikomo<br />

mfumu! Mulandira zimene mwanenazo. Koma nanga a<br />

Nthiwatiwa ndi a Mleme, kodi muchita nawo chiyani?”<br />

Kadzidzi anati, “Taonani mbali iyo, mukuona chiyani?<br />

Kodi si asirikali anga amenewa? Uyo wamkulu<br />

mimbayo ndiye mkulu wankhondo ndipo dzina lake<br />

ndi Fwipi. Ali kumbuyo kwakeko ndi Soka, nayenso<br />

ndi wodziwa za nkhondo. Onsewa ali ndi mipando,<br />

kaya udindo wa usajeni ali ndi thepe zitatu. Uyo ali<br />

chakunoyo pampandopo dzina lake ndi Apolo,<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

285


wachiwiri ndi Zenu, wachitatu ndi Tibo amene ali<br />

womalizira pa ulemu wa ankhondo anga. Ndanena izi<br />

kuti mukamva kuti a Mleme ndi a Nthiwatiwa<br />

zawavuta, mudziwe kuti nkhondo yake ndi imeneyi.”<br />

Inu nonse mukachita mwano, nkhondo ya ine Kadzidzi<br />

ndi imeneyo yolamulidwa ndi Sajeni Fwipi.<br />

Wolamulira ankhondo a Mfumu Kadzidzi, yemwe anali<br />

Sajeni Fwipi, ananyamuka ulendo wopita kwa Mleme.<br />

Atafika, Sajeni Fwipi analamula, “Apolo! Gwira Mleme!<br />

Mleme uyo! Akalimbalimba ipha!” A Mleme adagwidwa<br />

n’kutengeda ukaidi. Kenako anauyamba ulendo<br />

wopita kwa a Nthiwatiwa. Atafika, Sajeni Fwipi<br />

analamula, “Apolo! Gwirani msanga Nthiwatiwa uyoo!<br />

Akachita mwano, iphani!” A Nthiwatiwa nawonso<br />

adagwidwa n’kutengedwa ukaidi, ulendo wopita nawo<br />

kwa Mfumu Kadzidzi.<br />

Mfumu Kadzidzi ndi mbalame zonse panali<br />

kukondwera chifukwa cha kulimba mtima kwa Sajeni<br />

Fwipi, Sajeni Soka, Kopolo Apolo, Kopolo Zenu ndi<br />

Kopolo wang’ono Tibo pobweretsa achipongwe aja,<br />

odzikuza. Atafika nawo panali nkhani.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

286


Kadzidzi: “Kodi iwe Nthiwatiwa, bwanji sunabwere ku<br />

msonkhano? Sukudziwa kuti ine ndine mfumu?”<br />

Nthiwatiwa: “Zimenezo mukudziwa ndinu. Kodi si<br />

paja nyama zomwezi ndi zimene zidaveka ine ufumu?<br />

Kodi amene anakapala moto kwa Mfumu Tambala<br />

ndinuyo? Kodi mbalame zinazi sizikudziwa zimenezi?<br />

Funsani a Njovu kapena a Mvuwu akuuzani za ine!”<br />

Tsopano nkhani inavuta popeza mbalame zonse<br />

zidakumbukira za ufumu wa a Nthiwatiwa.<br />

Mleme: “Ine ndidamva moipa. Msonkhanowu amati<br />

ndi wa mbalame zokhazokha, kodi ine ndine<br />

mbalame? Kodi mbalame imakhala ndi mchira? Kodi<br />

mbalame imakhala ndi makutu? Kodi mbalame<br />

imakhala ndi pakamwa, mphuno ndi maso ngati<br />

mmene ndikuonekera inemu? Nanga miyendo yanga,<br />

kodi ikufanana ndi ya mbalame? Kodi ndili ndi<br />

nthenga ngati mbalame nonsenu? Eeeee?”<br />

Mfumu Kadzidzi idakanika kuyankha mafunso a<br />

Mleme ndipo zinali zochititsa manyazi zedi.<br />

Powafukula a Mfumu Kadzidzi, adasowa chochita<br />

ndipo panali umboni wokwanira wosonyeza kuti a<br />

Nthiwatiwa ndi amene anali Mfumu ya Mbalame<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

287


zonse. Ufumu wa a Kadzidzi unali wobera. Akadzidzi<br />

popsa mtima analamula ankhondo ake kuti aphe a<br />

Nthiwatiwa ndi a Mleme. Koma Sajeni Fwipi anati, “Ine<br />

kuyambira lero sindidzakuonaninso ngati mfumu.<br />

Ndiponso Sindingaphe m’bale wanga Mleme ayi.”<br />

Mbaleme zonse zinamuukira Kadzidzi ndipo nthawi<br />

yomweyo anathawira kuthengo. Kuyambira tsiku<br />

limenelo, a Kadzidzi amayenda ndi usiku kuopa<br />

kuonetsedwa mbwadza ndi mbalame zija.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi amene anali woyenera kukhala mfumu<br />

anali ndani?<br />

2. N’chifukwa chiyani Nthiwatiwa komanso Mleme<br />

sizinabwere kumsonkhanowu?<br />

3. Kodi zifukwa zimene anapereka zinali<br />

zomveka?<br />

4. N’chifukwa chiyani Kadzidzi amayenda usiku?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

288


Mkango ndi Bulu<br />

Kalekale Mkango utasowa nyama unasiya ana ake<br />

n’kupita kukasaka nyama. Koma Mkango sunasiyire<br />

ana akewo nyama yokwanira. Ndiye popita, unadzera<br />

kwa bwenzi lake Bulu.<br />

“Bwenzi langa, ine ndikupita kosaka, uzindionerako<br />

ana anga,” unatero Mkango. “Kodi mwawasiyira<br />

chakudya chokwanira?” Anafunsa Bulu. “Ayi<br />

n’chochepa, koma sindikakhalitsa,” unayankha<br />

motero Mkango ndipo kenako unauyamba ulendo<br />

wake.<br />

Patapita tsiku limodzi, Bulu anaona kunjira kuli zii.<br />

Patatha Sabata, Bulu mtima sanaupeze poganiza za<br />

ana a bwenzi lake Mkango.<br />

M’mawa wa tsiku lina, Bulu ananyamuka ulendo<br />

wokaona ana a mnzake. Pamene ankatulukira<br />

pamtunda, anadabwa kuona gulu la anyani pakhomo<br />

pa a Mkango, ana a Mkango ali m’manja mwa a<br />

Nkhwere, ndipo anafunsa kuti, “Kodi Anyani inu,<br />

munayamba kukhala ndi ana a Mkango?”<br />

Nyani wamkulu dzina lake Ziyenda anayankha kuti,<br />

“Kodi iwe Bulu wopanda nyanga, iwe ndiye mlonda wa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

289


a Mkango? Ana awa ife tatenga. A Mkango adayamba<br />

kale kudya ana athu. Ndiye lero tidya ana ake,<br />

kuphanga kwathu kotchedwa Dyero kuli phwando<br />

lero!”<br />

Bulu: “Kodi phanga limeneli lili kuti?”<br />

Ziyenda: “Waona phiri lili apolo? Yang’ana<br />

chakum’mawa kwakeko, kumeneko ndiye kuli phanga<br />

lathu, ubwere ndithu udzadye nawo.”<br />

Bulu: “Chabwino ndibwera, komanso mundikomere<br />

mtima ndibwere ndi mwana wanga wodwala.<br />

Asing’anga a Kalulu anati akudwala matenda a njala,<br />

ndiye atadya nawo phwandolo, akhoza kuchira.”<br />

Ziyenda: “Abwere ndithu.”<br />

Bulu: “Kodi kaphedwe ka mwana wa Mkango<br />

mumakadziwa?”<br />

Ziyenda: “Ayi!”<br />

Bulu: “He! Zikundu zanuzi zikhoza kunyeka zilonda,<br />

moti simungamathenso kukhala pansi. Chabwino,<br />

mundidikire ndidzaphe ndine!”<br />

Ziyenda ndi anzake anavomereza kuti amene adzaphe<br />

ana a Mkango ndi Bulu. “Chabwino, tatsogola<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

290


kukakonzeka. Udzapeza nkhuni zili ndu! kudikira iwe<br />

ndi mwana wako akudwalayo.”<br />

Pamene Bulu ankabwerera kwawo, anakumana ndi<br />

Mkango.<br />

Mkango: “Kodi m’bale wanga Bulu, watani? Nkhope<br />

yakoyi ngati ndi yokondwa!”<br />

Bulu: “Pepani ndithu kwagwa nkhondo. Ana anu onse<br />

awiri atengedwa ndi Ziyenda ndi anzake, anyani aja<br />

amakhala paseri pa phiri iloo!”<br />

A Mkango atamva zimenezi analira, “Vuuu! Vuuu! Ana<br />

anga ineee! Vuuu!” Koma a Bulu anati, “Musalire,<br />

zonse ndakonza kale.”<br />

Tsopano a Bulu analongosola zonse zimene<br />

zinachitika. Anafotokoza mmene anapezera Anyaniwo<br />

akutenga ana a Mkango. “Pepani bwenzi langa, ine<br />

ndawatchera msampha, lero lomwe ana anu<br />

tikawapeza ali moyo.” A Bulu analongosola zonse<br />

zimene adapangana ndi Anyani aja. “Inuyo<br />

ndikuberekani ngati mwana, ndipo tikafika kumene<br />

kuli ana anu. Tikakafika, mukhoza kukachita<br />

chilichonse chomwe mukuona kuti ndi chabwino!”<br />

Anatero a Bulu.”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

291


Atafika, Bulu anati, “Odi! Odi! Ndafika ndi mwana<br />

wodwala uja!” Ziyenda namuyankha kuti, “Lowani.<br />

Ana a Mkango aja ndi awa. Tikudikira kuti muwaphe<br />

kuti tiyambepo phwando lathu. Mwachitanso bwino<br />

kubwera ndi mwana wanu wodwalayu.”<br />

Nthawi yomweyo Bulu anati: “Dzimvere ntolo mwana<br />

wodwala! Zidze pano n’zatonse! Kadziwa mwini nkhuto<br />

wa Fulu!” Kenako a Mkango anatsika pamsana wa a<br />

Bulu. Anyani ataona kuti ndi Mkango, anadziwa kuti<br />

zinthu zasolobana. Anayesetsa kuthawa koma<br />

zachisoni, onse anagwidwa n’kuphedwa ndi Mkango.<br />

Ndiyendo a Mkango anati, “A Bulu, sindinkadziwa kuti<br />

ndiwe munthu wabwino chonchi! Ndiwe bwenzi langa<br />

la pamtima. Taona ana anga onse ali bwino. Tiyeko<br />

kumudzi ndikakupatse mphatso.”<br />

Atafika kumudzi, Mkango unati, “Kuyambira lero,<br />

uzigona m’nyumba kapena m’khola. Sudzagonanso<br />

pabwalo ngati nyama zina zonsezi.”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

292


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Anyani anagwira ana a<br />

Mkango?<br />

2. Kodi Bulu anawauza zotani?<br />

3. Kodi zinali zoona kuti anyani aja akapha<br />

mwana wa Mkango zikundu zawo zikhoza kunyeka<br />

zilonda?<br />

4. N’chifukwa chiyani Bulu anasiya kukhala<br />

m’tchire?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

293


Nkhuku ndi Nkhumba<br />

Tsiku lina Nkhumba inapita padzala. Nkhumbayi inali<br />

n’cholinga chokatoleza zakudya zotayidwa. Dzala<br />

limeneli linali la nyumba ya a Kamzati pamudzi wa<br />

Mawoneka. Pamene Nkhumba inkapita padzalalo,<br />

Khoswe n’kuti ali pompo kale, ndipo ataiona<br />

Nkhumbayo anabisala. Tsopano Nkhuku inabwera<br />

n’kuyamba kukambirana ndi Nkhumba.<br />

NKhuku: “Kodi Nkhumba, bwanji umavutika ndi<br />

zakudya za m’dzala ngati izi? Sizikutsegula m’mimba?”<br />

Nkhumba: “Inetu ndatha masiku ambiri mbuye wanga<br />

osandipatsa chakudya. Zikumveka kuti njala yalowa<br />

kudziko kuno.”<br />

Nkhuku: “Zoonadi, zimene mwamvazo n’zoona.<br />

Chimanga kulibe, gaganso kulibe.”<br />

Nkhumba: “Nanga iwe mnzanga umadya chiyani?”<br />

Nkhuku: “Ndimadya uchi wozuna.”<br />

Nkhumba: “Kodi uchiwo amakupatsa ndani?”<br />

Nkhuku: “Ine ndine wanzeru, bwenzi langa lina<br />

linandipatsa msampha wokolera njuchi ndipo zimaika<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

294


uchi mumsamphawo. Msamphawo umatchedwa<br />

mng’oma. Njuchi zimalowa m’menemo n’kuikamo zisa<br />

za uchi.”<br />

Nkhumba: “M’bale wanga, bwanji ukhale mnzanga?<br />

Ndigawireko uchiwo, taona ine mnzako ndikufa ndi<br />

njala! Taona nthitizi.”<br />

Nkhuku: “Mawa ukonzeke. Koma udzalawire chifukwa<br />

tidzayenda ulendo wautali kuti tikafike kumene kuli<br />

uchiwo. Ndiye popeza mng’omawo uli mumtengo,<br />

ndidzakuuza mmene udzachitire.”<br />

Tsopano Nkhumba inali ndi chimwemwe chodzadza<br />

tsaya itamva zimene nkhuku inamuuza. Koma Khoswe<br />

anabisala uja anamva nkhani yonseyi. Khosweyo<br />

anachita nsanje chifukwa nayenso njala inali<br />

itamuchita kanthu. Zimene ankaba usiku m’nyumba<br />

ya a Kamzati, sizinkapezekanso chifukwa cha njala ija.<br />

Khoswe mumtima mwake anati, “Hee! Tiona, ine<br />

sindingafe ndi njala Nkhumba itapeza mwayi wokadya<br />

uchi. Ndipita nawo komweko. Ndikulakalaka kutacha<br />

msanga kuti nanenso ndikaulawe.”<br />

Mmawa kutacha, Nkhuku ndi Nkhumba zidakumana<br />

padzala paja.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

295


Nkhumba: “Wadzuka bwanji bwenzi langa! Inetu<br />

ndafika kalekale pano. Paja akuluakulu adati, ‘Wamva<br />

m’mimba ndi amene amatsegula chitseko.’”<br />

Nkhuku: “Bwenzi langa, ndasangalala kuti<br />

wandilonjera chonchi. Koma tisachedwe, tiye<br />

tiuyambe. Pajatu ndinati uchiwo uli mumtengo! Ndiye<br />

. . .”<br />

Nkhumba: “Nanga ine ndikakwera bwanji<br />

mumtengowo. Inetu ndilibe mapiko ngati iwe!"<br />

Nkhuku: “Ayi inu a Nkhumba, musandidule<br />

pakamwa. Ndakuuzani kuti lero mukadya uchi,<br />

musakayikire iyayi. Nzeru zili ndi ine.”<br />

Nkhumba: “Ha! Ha! Ha! Lero kuli kudya!”<br />

Nkhuku: “Tamvera bwenzi langa. Ndikuuziretu, pali<br />

lamulo limodzi. Ine ndi iwe titenga nsungwi yaitali,<br />

ndiye iweyo ulume mbali imodzi, ine mbali inayo. Ine<br />

ndigwira ntchito youluka, ndipo iweyo unyamuka<br />

nawo limodzi. Tikafika mumtengomo, usakalankhule<br />

ndi wina aliyense. Ichi ndi chinsinsi chodyera uchi,<br />

timadya koma osalankhula. Koma wamvetsa za<br />

lamuloli?”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

296


Nkhumba: “Zamveka, ndikuona kuchedwa kwambiri<br />

kuti tinyamuke.”<br />

Pamene ankayankhula izi, Khoswe wa padzala uja<br />

ankangomvetsera. Tsopano Khosweyo anathamanga<br />

kwa bwenzi lake Khoswe wa patsidwi kukafunsa<br />

nzeru. Khoswe wa patsindwi anamuuza kuti,<br />

“Nkhumba imene ija ndi mdani wanga. Iweyo<br />

uwalondole, ndiye popeza wamva kale chinsinsi<br />

chawo, iwe upite n’kukaima patsinde la mtengowo.<br />

Uzikachita zinthu zoti zikamupsetse mtima. Ukaona<br />

akagwa n’kufa.”<br />

Mmawa kutacha, Nkhumba ndi Nkhuku zinayamba<br />

ulendo wawo. Zitafika pamtengo uja, Nkhuku inati:<br />

“Waona, mtengo uja ndi uwu. Mng’oma uja ndi uwo!<br />

Tsopano luma nsungwiyo. Konzeka m’bale wanga,<br />

limba mtima, tiye tsopano!”<br />

Nkhumba itaona kuti yakwera mumtengo inasangalala<br />

kwambiri, ndipo nkhuku inatenga uchi uja n’kuipatsa<br />

Nkhumba ndipo onse anayamba kudya. Mwadzidzidzi,<br />

pansi panamveka mawu a Khoswe, “Ha! Chitsiru iwe<br />

Nkhumba wodya zowola, tsika! Kadye zowola zako<br />

kudzala! Tsika chitsiru iweeee!”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

297


Nkhumba inamva izi, mtima wake unayaka moto<br />

ndipo inaiwaliratu lamulo lija loti asamayankhule<br />

akudya uchi. Kenako inati, “Aaa! Kamwana ngati iwe<br />

sungandichite chipomwe chotere. Kodi ndikudya<br />

zako?” Mawu amenewa ali m’kamwa, nthambi ya<br />

mtengo umene Nkhumba inakhala inakhadzuka ndipo<br />

Nkhumba inakuwa kuti, “Hi! Bwenzi langa ndikufa!”<br />

Nkhumba inagwera pansi kuti phii!<br />

Nkhuku itaona zimene zinachitkazo inati: “Oooo!<br />

Bwenzi langa tsokalo, tsokaloo!”<br />

Kenako Khoswe anapita pamene panagwera Nkhumba<br />

paja n’kunena kuti, “Ndinakuuza ndiwe chitsiru,<br />

tachionani chatsakamuka chili gaada! Chimati chitani<br />

chikadya za m’dzala!”<br />

Nkhumba idagwa ndi chipumi moti mphuno yake<br />

idanyindukiratu. Mphuno ya nkhumba inaonongeka<br />

kwambiri chifukwa cha dyera la uchi komanso<br />

kusamvera malamulo.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

298


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani nkhumba inakwera<br />

mumtengo?<br />

2. N’chifukwa chiyani mphuno ya nkhumba ndi<br />

yophwanyika?<br />

3. Kodi dyera komanso kusamvera malamulo<br />

kumabweretsa mavuto otani?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

299


Ng’oma ya Kalulu<br />

Kalulu adali ndi bwenzi lake lapamtima. Bwenzi lakeli<br />

linali Nkhandwe. Tsiku lina Kalulu anaona bwenzi<br />

lakeli likubwera potero. Pa nthawiyi Kalulu ankaotha<br />

moto ndipo n’kuti dzuwa likulowa. Bwenzi lake lija<br />

litafika, Kalulu anakondwa kwambiri ndipo anakonza<br />

zakudya kuti bwenzi lake lisangalale.<br />

Atatha kudya Chakudya, Kalulu anati, “Kodi<br />

mwangotiyendera?” “Ayi bwenzi langa, ine<br />

chandiyedetsa ndi chinthu. Koma ndisanayambe<br />

kulongosola, ndikufuna undiuze mayina a adani ako<br />

onse.” Inatero Nkhandwe. Inkafuna kuti iitane adani a<br />

Kaluluwo kuphwando kuti adzawakhaulitse.<br />

Tsiku la phwandolo litakwana, Njovu, Mkango ndi<br />

Kadyamsonga zidafika kunyumba kwa Kalulu.<br />

Madyerero anayambika, ndiye popeza nthawi idali<br />

itatha, onse adagona. M’mawa kutacha, phwando<br />

linayambanso.<br />

Nkhandwe: Akuluakulu, phwando likayamba, Kalulu<br />

atenga ng’oma iyo n’kuyamba kuimba ndipo tonse<br />

tizivina!<br />

Njovu: Eya! Ilitu ndiye phwando, lochita kuthudzulira<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

300


gule! Nanga paphwando pazichita kukhala ngati<br />

pamaliro?<br />

Mkango: Ndipo inuu! Tiyeni timasuledi ziuno! Mwina<br />

zingachoke dzimbiri.<br />

Kadyamsonga: Koma ndiyetu timuponda gule!<br />

Kenako anapatsidwanso nsimba yangati phiri ndipo<br />

akuluakuluwa anakhala moizungulira. Anaipwekeka<br />

koopsa moti onse anakhuta mimba tugululu, ndipo<br />

anapempha Kalulu kuti ayambe kuwaimbira ng’oma.<br />

Kalulu atayamba kuimba ng’omayo, nyama zonse<br />

zinayamba kuthimbwidzika, nthawi yomweyo Njovu,<br />

Mkango ndi Kadyamsonga, adangozindikira kuti<br />

ayamba kumira m’nthaka ngati kuti ali pamadzi.<br />

Pamene Kalulu anaona zimenezi analimikira kuimba<br />

ng’oma ija. Apono ndiye zinthu zinavuta.<br />

Njovu: Iwe Kalulu, tipulumutse, taona tikumira<br />

munthaka.<br />

Mkango: He! Kalulu, pepa, tipulumutse chonde<br />

tikumira m’nthaka.<br />

Kadyamsonga: Pepa! Pepa Kalulu, Kaluluuuu!<br />

Tipulumutse chondeeee!<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

301


Kalulu: Hehee! Ndiwedi bwenzi langa Nkhandwe!<br />

Waziona mfitizi, zatha lero! Ndizionetsa polekera.<br />

Nkhandwe: Imbitsa! Imbitsa! Imba m’bale wanga<br />

akhaule amenewa!<br />

Njovu: Mayo! Mayoooooo! Tikufa kunoooo! Kalulu,<br />

ndakweza manja anga ndagonja!<br />

Mafunso:<br />

1. Mukuganiza kuti n’chifukwa chiyani Kalulu<br />

anaitana nyama zija?<br />

2. Kodi n’chiyani chinachititsa kuti nyamazi<br />

zimire munthaka?<br />

3. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

302


Ubwenzi wa Njovu ndi Mkango<br />

Kalekale kunkhalango yotchedwa Kambirira pafupi ndi<br />

midzi ya m’dziko la Kabango kunali nyama ziwiri<br />

zokondana kwambiri. Nyamazi zinali Mkango ndi<br />

Njovu. Munkhalangoyi munalinso nyama zina zambiri.<br />

Komabe Mkango nthawi zonse unkangokhala<br />

wachisoni chifukwa unali wokalamba moti unkasowa<br />

mphamvu zogwirira nyama. Nthawi zambiri<br />

unkangokhalira kugona nayo njala chifukwa chosowa<br />

chakudya. Mwamwayi unali ndi bwenzi lake Njovu.<br />

Kawirikawiri Njovu inkapereka mphatso ya nyama kwa<br />

Mkango.<br />

Mkango unkatenga chitete m’mamawa kuli mbuu,<br />

ulendo kukaba maungu m’minda ya anthu. Madzulo<br />

unali ulendo kukapereka maunguwo kwa bwenzi lake<br />

Njovu.<br />

Mwatsoka, chaka china kunasowa mvula ndiye<br />

zachisoni, kunali njala ya mtima bi. Tsiku lina Njovu<br />

ndi Mkango anayamba kukambirana. Mkango unati,<br />

“Bwanawe Njovu, ine masiku ano ana anga akufa ndi<br />

njala. Pakadapanda iwe, tonse bwenzi tili mitembo.”<br />

Koma zinthu zafika posauzana chifukwa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

303


chimkukuluzichi chagwedeza aliyense. Koma kaya<br />

chaka chino tigwira mtengo wanji? “Pepa bwenzi<br />

langa. Chimkukuluzi changati chimenechi ine<br />

ndinachionaponso, ndikuganiza kuti pa nthawiyo<br />

n’kuti iwe usanabadwe. Nthawi imeneyo agogo ako<br />

ndidawaona akudya msipu. Ndipo atete anga<br />

ndidawaona ndi maso angawa akudya nyama. Ndiye<br />

zimene zatigwera chaka chinozi ndikuona kuti<br />

zikulondola mapazi omwewo. Ayi, tiona mmene<br />

zithere. Zikomo!” Inatero Njovu.<br />

Atalekana aliyense anaona msana wa njira. Mkango<br />

utayenda pang’ono unadzera njira yachidule yodutsa<br />

m’tchire. Mwadzidzidzi utatulukira pena unangoona<br />

chimunda cha maungu chili thee! Maungu ali<br />

ngundangunda. Nthawi yomweyo unalankhula<br />

chamumtima nuti, “Ndibwerere ndikauze bwenzi langa<br />

kuti laponda diwa la mphawi, kuli maungu uku!”<br />

Mkango unabwereradi ndi liwiro loopsa. Kenako,<br />

unaona Njovu ikupita potero ndipo unati, “Eeeyi, Ima<br />

pomwepo bwenzi langa ndakupezera maungu!”<br />

Pamene Njovu inamva mawu amenewa inatembunuka<br />

niti, “Kodi n’zoona zimenezo?” Kenako Njovu inayamba<br />

ulendo wopita kumene kunali munda wa maungu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

304


kuja. Atafika pamtunda pamene amapenukira<br />

kumatsitso kumene kunali munda kuja, Njovu inaona<br />

kuti ndi zoona, nkhani ya maungu ija inalidi yoona<br />

ndipo inati, “Zikomo ndithu bwenzi langa,<br />

wandipulumutsa! Tsopano ndithamange liwiro loopsa<br />

kuti ndikapeze mtendere, mundipeza.” Mosachedwa<br />

Njovu inaliyatsa liwiro lothyola nalo mitengo.<br />

Zachisoni pamene Njovu inafika pamunda paja inaona<br />

kuti maungu onse anali owola kwambiri. Zitatero<br />

m’maso mwa Njovu munayamba kulengeza misozi.<br />

Pamene Mkango unkafika unadabwa kuti bwenzi lake<br />

likulila ndipo unati: “Kodi bwenzi langa ukulira<br />

chiyani?” Njovu inati, “Taona maungu aja ndi owola<br />

okhaokha.” Mkango unati, “Aaaa, kodi ndizo<br />

zachitika? Pepa kwambiri. Ili ndi tsoka. Mdani wathu<br />

ndi amene wawoletsa maungu amenewa.”<br />

Njovu inabwerera kwawo ili ndi njala ndiponso<br />

chisoni. Ulendo uli mkati, Njovu inapeza Njati yakufa<br />

ili gadaaa. Njovu inati ndikauza bwenzi langa kuti<br />

ndamupezera mwayi.<br />

Njovu inaliyala liwiro kuthamangira Mkango.<br />

Posachedwa inafika nipeza Mkango utagona pansi<br />

ukubuula ndi njala ndipo njovu inati, “Bwenzi langa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

305


dzuka, kodi watani?” Mkango unayankha kuti, “Pepa<br />

bwenzi langa, ine ndinakomoka ndi njala. Tsopano<br />

imfa yafika moti miyendo yanga ali m’kamwa mwa<br />

ng’ona. Sindikhala ndi moyo ayi.” Njovu inati,<br />

“Dzukani tsopano, ndakupezerani chinyama cha Njati<br />

cha mafuta noninoni.”<br />

Mkango utangomva mawuwa, unangoti, mbalanganda!<br />

Kudzuka, ndipo unathamangira kumene kunali Njati<br />

kuja. Utafika, unangopeza ntchentche zokha zili<br />

m’matsekera zili ng’waaaa. Anthu auzimba<br />

anaipezerera nyama ija, n’kutengeratu yonse. Njovu<br />

inati, “Pepa bwenzi langa, ona mapazi a anthu awa.<br />

Atenga nyama ija ife tili m’njira.”<br />

Tsopano Mkango lilime lake linasololoka, dovu<br />

n’kumangochucha ndipo kenako unagwa pansi<br />

n’kukomoka. Posachedwa Njovu inayamba<br />

kunjenjemera. Nayonso inagwa pansi n’kukomoka.<br />

Kenako mumsewu munkadutsa chigulu cha anthu<br />

ochokera kumsika. Anthuwa anali atatenga zitete<br />

zodzaza ndi maungu, nyama, ufa, chimanga, dzombe<br />

ndi zina. Chifukwa cha phokoso, Njovu ndi Mkango<br />

zinatsitsimuka, tsopano anamva kuyankhula. Atautsa<br />

mitu yawo, anaona kuti anthuwo anasenza zinthu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

306


zabwino zokhazokha. Njovu inati, “Bwanawe, tapeza<br />

mwayi tsopano. Tisasauke ayi. Tikhalebe chogona<br />

ngati tafa. Tikhoza kuwalanda zinthu atengazi.<br />

Mkango unati, “Khala chete, tsopano mwayi wathu ndi<br />

umenewu.”<br />

Munthu wina anati, “Anzathu, onani Mkango ndi<br />

Njovu zaphana! Lero tapeza mwayi, tiyeni titule<br />

katunduyu kuti tichekerane nyama zakufazi.”<br />

Anthu onse anatula pansi katundu wawo, nayamba<br />

kuthamangira nyama zija. Mkango ndi Njovu,<br />

zinadzukira pamodzi kuti, mbalanganda, mkango<br />

umvekere, “Vuuu! Vuuu!” nayonse njovu imvekere,<br />

“Kherrrr! Kherrr!” Anthu aja amvekere, “Mayo mayo<br />

mayo ineeeeeee! Tikufa kunoooooo!”<br />

Anthu aja atathawa, Njovu ndi Mkango zinakhala<br />

pansi n’kuyamba kudya zimene anthuwo anasiya.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

307


Mafunso:<br />

1. N’chiyani chikusonyeza kuti njala inali itafika<br />

poipa kwambiri?<br />

2. Kodi n’chiyani chikusonyeza kuti Mkango ndi<br />

Njovu zinali mabwenzi okondana kwambiri?<br />

3. Kodi nyamazi zinatani kuti zipeze chakudya?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

308


Kalulu Aphetsa Ana<br />

M’dziko lotchedwa Fukizi munali munthu wina amene<br />

anali wolimbikira kulima mtedza. Munthuyu dzina<br />

lake anali Bikoko.<br />

Mtedza utacha, Bikoko anaona mapazi anyama za<br />

mtchire. Pambuyo, anaona kuti mtedza wake<br />

unayamba kuwonongeka. Nyama zambiri zinali<br />

kuwononga zokolola zake. Nyama zimene<br />

zimawononga sankazidziwa kwenikweni. Motero,<br />

anaganiza kuti akabisale kuti aone nyama zimene<br />

zinali kuwononga zokolola zake. Bambo Bikoko<br />

anakhala m’chisimba chake koma sanaone nyama<br />

iliyonse.<br />

Kalulu anangoti m’munda muja, tulukiru! Maso<br />

mwazumwazu! Kenako anaona mwini munda ali<br />

m’chisimba. Kalulu uja anayenda mochenjera kuopa<br />

kuonedwa ndi mwini munda. Tsopano anatenda<br />

dzungu n’kuliboola, iyeyo n’kulowa m’menemo ndi<br />

kulivundikira bwino kuti wina aliyense asamuone.<br />

Bambo Bikoko anatopa tsopano, ndipo anaganiza<br />

zopita kumudzi kukapumula. Atangochoka, njovu<br />

inafika nitola dzungu lija munali Kalulu, n’kumeza.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

309


Njovu ija ili kuyenda, Kalulu anazindikira kuti ali<br />

m’mimba mwa Njovu ndipo anati, “Lero kuli phwando,<br />

n’kutere zamkati kunona!” Kalulu anatulutsa mpeni<br />

wake n’kudula mtima wa Njovu. Nthawi yomweyo<br />

Njovu inagwa, n’kuferatu.<br />

Tsopano Kalulu ataona kuti Njovu yafa, anatulukira<br />

kukamwa kwake ndipo mosachedwa anatenga mpango<br />

nayinjata nsangamutu.<br />

Nthawi yomweyo Kalulu anaona anthu a uzimba ali<br />

kupha ziwala. Kalulu anakwera pachulu nayamba<br />

kukuwa nati: “He kodi imeneyo ndi nkhuli?” Anthu aja<br />

anamuona Kalulu uja, nayamba kum’thamangitsa,<br />

koma kalulu anazungulira chitsamba, n’kulowa<br />

m’mimba mwa Njovu ija ndipo a uzimba aja atafika<br />

pafupi ndi Njovu, Kalulu anayamba kubuwula. Anthu<br />

aja anayifunsa Njovu ngati inaona Kalulu, koma Njovu<br />

inati: “Pepani abale anga ine sindili bwino ayi. Litsipa<br />

landivuta kwambiri.” Anthu aja anabwerera<br />

osamuowona Kalulu, kenaka, Kalulu anatulukanso,<br />

n’kukwera pachulu chija nati: “Nkhuliyo m’dambomo!”<br />

Kalulu analowanso m’mimba mwa Njovu yakufa ija.<br />

Tsopano anthu aja anatopa naye Kalulu ndipo<br />

anaganiza zoika mlonda kuti aone chinsinsi cha<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

310


Kalulu ndipo anaika mlonda pa chitsamba pafupi ndi<br />

Njovu ija. Anthuwo atachoka, Kalulu anatulukanso<br />

n’kukwera pachulu nati, “Nkhuliyo m’dambomo!”<br />

Atatero anakalowanso m’mimba mwa Njovu ija,<br />

mlonda uja akuona zonse zomwe zinkachitika.<br />

Mlondayo anaona kuti polowa m’mimba mwa njovu<br />

analowera pakamwa ndipo anamva Kaluu akubuula<br />

m’mimba mwa Njovumo.<br />

Mlonda uja anaubutsa ulendo kupita kwa anzake aja<br />

nawauza kuti chinsinsi cha Kalulu chimene<br />

anachipenya. Anaulula kuti Kalulu akumathawira<br />

m’mimba mwa Njovu ndipo akumayamba kubuula,<br />

kutiphimba m’maso kuti tiziti ndi Njovu ili kubuula.<br />

Anzake aja anati, “Hi! Talekerera nyama!” Ndipo<br />

ananyamuka n’kupita pamene panali nyama paja<br />

mipeni ili m’manja kukayamba kucheka nyama ya<br />

Njovu. Kalulu atamva kuti anthu aja ayamba kuicheka<br />

Njovu ija, analimbikira kubuula: “Mayo ine! Ha!<br />

Haaaaaaa! Litsipa ine. Litsipa ineee! Nditani inee!<br />

Kandifunireni mankhwala anthu inu! Ndili ndi moyo<br />

anzanga inuu.” Mlonda uja anati, “Bodza, bodza! Ndi<br />

Chikalulu!”<br />

Pamene Kalulu anamva mawu amenewa, basi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

311


anadziwa kuti zake zada. Tsopano anaganiza nzeru<br />

ina. Iye anati, “Tsopano anthu amenewa anditulukira,<br />

ine zimene ndichite, iwo asanandipeze, ndilowe<br />

m’chifu cha Njovuchi.” Kalulu anabisala m’chifu cha<br />

Njovu.<br />

Anthu aja ataiboola Njovu ija m’mimba, anaona kuti<br />

mulibe Kalulu. Bikoko mtsogoleri wawo anati, “Kodi<br />

iwe mlonda, suja umanena kuti m’mimba mwa Njovuyi<br />

muli Kalulu? Nanga ali kuti?” Mlondayo anati,<br />

“Bwana, ntchito yopeza zinsinsi za Kalulu ikadalipo.<br />

Ine ndapusa koma wopusa sadziwika. Uyu Kalulu<br />

timamudziwa tonse.” Bikoko anati, “Chabwino, ine<br />

udziwa ndimakonda chifu cha Njovu, chifukwa<br />

mumakhala maungu ophikika bwino, chitenge upatse<br />

mwana wanga Bwasano uyo, akapereke kwa amake<br />

kuti akaphike.” Chifu chija anachitenga Bwasano<br />

kupita nacho kumudzi.<br />

Ali panjira, mwana uja anamva kuti chifu<br />

chikuyankhula, “Taya! Taya! Fulumira tayaa!”<br />

Bwasano atamva zotere, zinamudodometsa ndipo<br />

anataya chifu chija n’kuyamba kuthawa.<br />

Nthawi yomweyo Kalulu anatuluka, mwana uja<br />

osadziwa, ndipo anathyola masamba a mtengo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

312


wotchedwa kafwito nasunga m’manja. Munthu<br />

akangotafuna masambawa amagona tulo tofa nato<br />

tsiku lathunthu. Kalulu anauza Bwasano kuti, “Bwera<br />

kuno! Bwera kunooo!” Mnyamata uja anacheuka,<br />

ndipo anabwerera.<br />

Kalulu: Kodi umathawa chiyani?<br />

Bwasano: Chifuchi chimayankhula.<br />

Kalulu: Ayi wayamba misala iwe, tenga mankhwalawa<br />

utafune m’kamwa mwakomo ndiye pafunika kuti<br />

upumule, usayendenso ayi, tsopano lowa m’chifumo<br />

ukakhale pansi, ine ndikunyamula. Ine ndine<br />

sing’anga oposa onse. Lowa msanga!<br />

Bwasano analowa m’chifu chija ndipo Kalulu<br />

ananyamula chifucho ulendo kwa mkazi wa Bikoko.<br />

Atayandikira, Kalulu anafunsira za nyumba ya a<br />

Bikoko, ndipo anauzidwa mmene angakafikire<br />

kunyumbako.<br />

Atatulukira pamudzipo anaona nyumba imene inali<br />

ndi chikwere cha nkhunda pabwalo ndiponso panali<br />

mitengo itatu ya naphini, ndiyeno anati, “Monga muja<br />

andiuzira anthu, nyumba ya Bikoko ndi imeneyi.”<br />

Kalulu anaodira, “Odii! Odii!” Mayi onenepa aafupi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

313


koma oyera, atsitsi la nzindo anatulukira koma<br />

nkhope ili yachisoni.<br />

Kalulu: Kodi Mayi, ndinu amayi a kwawo kwa a<br />

Bikoko?<br />

Mayi: Eee!<br />

Kalulu: Bwanji osakondwera ndi chimtengatenga<br />

ndatengachi?<br />

Mayi: Ayi a Kalulu, ine ndili pachisoni chachikulu.<br />

Kuno kuli matenda banja lonse ngakhale inenso<br />

m’thupimu simwanga ayi. Ana athu awiri Diroli ndi<br />

Chisangwi onse ali gonire, moti a Bikoko ndiponso<br />

Bwasano sakudziwa zimenezi. Ndangokhala ndekha,<br />

ndiye ndangoti ndodo mtolo!<br />

Kalulu: Pepani mayi koma limbikirani kuwafunira<br />

zitsamba zonse zili m’tchirezi. Mayi ine ndatumidwa<br />

ndi Bambo Bikoko kudzatula chimtengatengachi. Iwo<br />

akuti mutenge chimtsuko chachikulu ndipo miyikemo<br />

chifuchi osachidulayi. Akuti muli maungu awo ndipo<br />

akufuna apsere m’chifu chomwechi. Anatero<br />

malamulo awo a chifuchi. Ndiponso akuti mundiphere<br />

nkhuku popeza ndanyamula chifu chawochi.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

314


Amayi aja msangamsanga chifu chija anachiika<br />

m’chimphika chachikulu, naika pamoto. Anaphanso<br />

nkhuku naika mumphika waung’ono. Nsima<br />

inaphikidwa ndipo Kalulu anadya nsima ija ndi nyama<br />

ya nkhukhu. Kalulu anasonkhanitsa mafupa onse<br />

n’kusunga ali, “Chimapulumutsa munthu<br />

sichidziwika.” Kenako anauza mayi aja kuti, “Pepani<br />

mayi ine m’thupimu sindikumva bwino, ndimati<br />

ndipemphe malo ogona.”<br />

Nthawi yomweyo mayi uja anatenga nsalu yakuda<br />

n’kumupatsa Kalulu nati, “Bwerani kuno mugone<br />

pamodzi ndi Diroli ndi Chisangwi, iwe ugone pakatipo.<br />

Mungogonera limodzi popeza mphasa yapadera palibe.<br />

Ndadziwa wadwala chifukwa unanyamula katundu<br />

wolemera kwambiri.”<br />

Kalulu anagona pakati paja nafunda nsalu yakuda<br />

koma Diroli ndi Chisangwi anafunda nsalu zoyera.<br />

Amayi aja ali kusonkhezera mphika uja, chimoto chili<br />

lilili! kuyaka, chimphika chija chili, bwata! bwata!<br />

kubwatitsa chifu cha a Bikoko. Nthawi yomweyo a<br />

Bikoko anafika ndipo anafunsa, “Kodi chifu chafika?”<br />

“Zoona, chifu chafika ndi Kalulu,” anayankha motero<br />

amayi aja. “Aa! Chafika ndi Kalulu! Kodi ine ngati<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

315


ndinatuma Kalulu, ine ndinatuma Bwasano osati<br />

Kalulu ayi,” anatero a Bikoko. “Hi! zanu izooo, Kalulu<br />

ndiye wabweretsa.” Anayankha motero amayi. “Bwanji<br />

waphika motere chifu changa? Kodi chifu amaphika<br />

osafinya? Mkazi wosadziwa kuphika iwee!” Anazaza<br />

motero a Bikoko. “Ndachita motsata malamulo anu,<br />

anandiuza zimenezi ndi Kalulu,” anayankha motero<br />

mayi aja.<br />

Nthawi imeneyi Kalulu ankamva phokoso lija, tsopano<br />

anasuntha malo, anagona kumbuyo kwa Chisangwi,<br />

ndiye kuti Chisangwi, anali pakati tsopano, nsalu<br />

anatenga yoyera ya Chisangwi ndipo Chisangwi<br />

anamufunditsa yakuda ija ali, “Ee! Tione mmene<br />

zikhalire.”<br />

Bikoko: Tenga mpeni toboole chifuchi tichifinye, kuti<br />

tiphikenso bwino.<br />

Mkazi wa Bikoko: Kodi mukufuna kuona maungu<br />

anuwo?<br />

Bikoko: Maungu ati?<br />

Mkazi wa Bikoko: Akuti muli maungu anu mmenemu<br />

n’chifukwa chake mumati tiphike chotere.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

316


Bikoko: Amatero ndani?<br />

Mkazi wa Bikoko: Inuyo! Kodi chifuchi ndimayesa<br />

chachokera kwa inu? Nanga ine ndikadangochita za<br />

m’mutu mwanga?<br />

Bikoko: Zonse n’zabodza, Kaluluyo wapita kuti<br />

ndimufunse.<br />

Mkazi wa Bikoko: Wadwala, wagona pakati pa Diroli<br />

ndi Chisangwi kuchipinda cha ana, wafunda nsalu<br />

yakuda ija.<br />

Bikoko: Phula mphika! Tenga mpeni ting’ambe,<br />

tiphikenso titafinya.<br />

Bikoko anatenga mpeni nang’amba chifu chija. “Ooo!<br />

Mayo! Mayoo! Mwana wangaaa!” Anaona Bwasano<br />

wophikika atafa kale. Amayi anafunsa, “Kodi<br />

n’chiyani?” Bikoko anati: “Hii! Mwana wapsa! Waphika<br />

Bwasano!” Bambo analira. Amayi anathamanga kuti<br />

akaone, “Mayo! Mayo! Mayo! Nkhondoyoo!” Bikoko<br />

anati, “Patse uta wanga! Lero naye akufanso!” Onse<br />

analowa m’chipinda chija.<br />

Mkazi wa Bikoko: Kalulu ndi uyo ali pakatiyo.<br />

Mlaseni!<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

317


Bikoko: Aona polekera lero, ndimukhomerera pansi<br />

ndi muviwu!<br />

Wodwala: Mayo atate mwandipha!<br />

Tsopano Kalulu bzunthu! waliutsa liwiro.<br />

Povundukula nsalu yakuda ija anaona ndi Chisangwi,<br />

ali, thinuuu! thinuuu! kusauka ndi imfa. Bikoko anati,<br />

“Hii! Ndapha mwanaa!” Waliyatsanso liwiro<br />

kuthamangira Kalulu. Tsopano Kalulu anatsekula<br />

liwori lake lomaliza agalu ali taaawaaa! Kalulu anaona<br />

kuti zinthu zavuta popeza agalu ena anamubzola<br />

ndikum’dulizira kutsogolo, Kalulu anatenga mafupa a<br />

nkhuku aja n’kumawatayira, ndiye agaluwo<br />

akadachedwa ndi kulimbirana mafupa iye anangoti<br />

khophe! wapita. Nafenso tiyenera kuchenjera ndi<br />

anthu a maonekedwe ngati a Kalulu.<br />

Mafunso:<br />

1. N’chifukwa chiyani Kalulu analowa m’kati mwa<br />

dzungu?<br />

2. Kodi anapezeka bwanji m’kati mwa chifu?<br />

3. Kodi khalidwe lakeli linaphetsa bwanji ana?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

318


Ubwenzi wa Kalulu ndi Fisi<br />

M’dziko la Nsabwe, munali akazi awiri amene<br />

ankafuna kukwatiwa ndi nyama zam’tchire. Adaganiza<br />

zimenezi chifukwa akaziwa ankaona m’mene akazi<br />

anzawo ankazunzidwira ndi amuna awo. Maina a<br />

akaziwa anali Khumbo ndi Mtimaukanena.<br />

Nyama zam’tchire zinamva za mbiriyi. Posakhalitsa<br />

nyama zamitundumitundu zinayamba kubwera kwa<br />

Nsabwe koma zambiri zinalephera mbeta za akazi<br />

awiri aja. Tsiku lina a Njovu, a Njati ndi a Mkango<br />

adapitira limodzi kukayesa nawo kufunsira mbeta zija.<br />

Njovu: Kodi iwe Mtimaukanena, ine ukandiona,<br />

umandiona bwanji? Sumandigomera? Kodi mwamuna<br />

ukufunayo, amaposa ife a Njovu? Pofuna amuna<br />

muzisankha ife amphamvu, a mangolomera.<br />

Mtimaukanena: Pepani a Njovu. Mtima wanga<br />

sunandiuze kuti ndikuvomereni ukwati ayi.<br />

Njovu: Chabwino, tabwera iwe Khumbo, kodi<br />

ndimayesa kuti mukufuna ife nyama zam’tchire,<br />

tabweratu kwa ife a Njovu. Kodi simukukhutira nane?<br />

Khumbo: Ayi a Njovu, mtima wanga sunakhumbe inu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

319


ayi.<br />

Njovu: Atsikana awirinu, zedi mwataya mwayi, tsiku<br />

ndi tsiku bwenzi mukudya maungu mukanalola ine.<br />

Khumbo: Hoo! Zakuba m’minda mwa enizo! Toto ine<br />

kukwatiwa ndi chimbala! Anthu ambiri anapunduka<br />

chifukwa chakudya zotsirika. Toto ifee!<br />

Tsopano a Njovu anatuluka nauza anzake aja kuti:<br />

“Anzanga, tangovutika, anamwaliwa ndi okongola<br />

koma ndi ovuta. Tangotaya nthawi pachabe kubwera<br />

kuno.” A Mkango anati, “Ine sindingangobwerera<br />

kunjira pokhapokha nane nditayesa mwayi wanga,<br />

zichite kukakanikira komweko.”<br />

Mkango: Odii atsikana, tabwera ife amunamuna, a<br />

Mkango odya nyama tsiku ndi tsiku. Si za aja a Njovu<br />

odya mawungu akuba ayi. A Mtimaukanena,<br />

mukuganiza bwanji za ine? Bwanji ndinkhale<br />

mwamuna wanu?<br />

Mtimaukanena: Pepani a Mkango, mtima wanga za<br />

inu sunanene kuti mukhale mwamuna wanga.<br />

Mkango: Nanga iwe Khumbo? Ukuti bwanji?<br />

Khumbo: Ayi, pepani, mtima wanga sunakukhumbeni<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

320


mpang’ono pomwe.<br />

A Mkango anapsa mtima ndipo anangotuluka<br />

m’nyumba muja. Atafika kwa anzake anati,<br />

“Anzanganu, basi tiyeni tizipita kwathu. Ukaona<br />

mtengo wauwisi ukuyaka, nanga wouma n’kutani?<br />

Kwenikweni inu ongodya msipu mumtsinje, ha!<br />

Sangakuwerengereni n’komwe, akhoza<br />

kukangokutukwananiko. Tiyeni tizipita.”<br />

Mbiri inamveka m’mkhalango yonse kuti zinthu<br />

zavuta. Onse akuluakulu atatu akanidwa ndi mbeta<br />

mochititsa manyazi. Kalulu ndi Fisi anawawidwa<br />

mtima. Tsiku lina Fisi ananyamuka kupita kwa akazi<br />

aja.<br />

Fisi: Zikomo! Zikomooo! Tafika ife amuna osaopa<br />

mdima, oyenda usiku ndi usana. Ndabwera<br />

kudzafunsira ukwati nonsenu, ndikufuna ndikhale ndi<br />

akazi awiri. Nanga muli ndi mawu?<br />

Mtimaukanena: Mtima wanga wanena kuti mwamuna<br />

amene ndakhala ndikuyembekeza ndinu. Ndavomera!<br />

Khumbo: Inenso, mtima wanga wafera inuyo basi! Inu<br />

a Fisi ndiye taona kuti mukhale mwamuna wa ife<br />

awiri.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

321


Fisi: Chabwino, ndikukatenga nkhoswe yanga kuti<br />

tigwirizire chinkhoswe. Sindifuna ukwati wachabe,<br />

wongotengana popanda chinkhoswe ngati amachitira<br />

enawa.<br />

Mbiri inamveka m’nkhalango monse kuti Fisi ndiye<br />

amene waloledwa kukhala mwamuna wa akazi awiri<br />

aja. Nyama zonse zinali zododoma popeza Fisi ndi<br />

wakuba, wodya zoola komanso zakufa. Fisi atafika<br />

kwa Kalulu, anafotokoza monga mmene zinayendera.<br />

Kalulu anavomera kukhala nkhoswe ya Fisi.<br />

Tsiku la Chinkhoswe lisanafike, Kalulu anangolawira<br />

kuti akukasamba kumtsinje, koma unali ulendo<br />

wopitakwa akazi aja. Atafika Kalulu anati, “Tamva kuti<br />

mwalola Fisi kuti akhale mwamuna wanu nonsenu.<br />

Akazi opanda nzeru ngati inu sindinawaonepo. Kodi<br />

simudziwa kuti Fisi amadya zoola, zongofa zokha<br />

komanso ndi wauve koopsa? Simudziwa kuti Fisi ndi<br />

bulu wanga?”<br />

Kalulu: Nanga inu mwafera chiyani? Fisi ndi mbala<br />

yoopsa. Amachita mgoneko usiku ulionse. Mbuzi,<br />

nkhumba za anthu zatha phu! Kuti apeze chakudya<br />

chaufulu, ayi, ntchito ndi kuba m’midzimu. Amene uja<br />

ndi bulu wanga. Kodi simukudziwa zimenezi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

322


Khumbo: Ayi sitidamvepo. Koma inuyo mutitsimikizire<br />

kuti a Fisi ndi bulu wanu. Mukachita zimenezo, ife<br />

tidzasintha mtima ndipo tidzakwatiwa ndi inu a<br />

Kalulu.<br />

Kalulu anabwerera kwa bwenzi lake Fisi. Tsiku la<br />

chinkhoswe linafika, ulendo unali mkati wopita kwa a<br />

Nsabwe. Atatsala pang’ono kufika, anafika pamtsinje<br />

wina. Kalulu anathamangira madzi a mumtsinjewo<br />

n’kuyamba kumwa. Fisi anafunsa, “Kodi ukumwa<br />

madzi nthawi zino bwanji?” Kalulu anayankha kuti,<br />

“Ndiye kuti ndayamba kudwala m’bale wanga,<br />

sindithanso kuyenda ayi. Pepa bwenzi langa,<br />

tifulumire kukatula mbetayi ndiponso lero lomwe<br />

tikagwirire ndithu chinkhoswe. Ine ndine nkhoswe<br />

yako ya kuchimuna. Tsono miyendo yanga, yauma,<br />

sinditha kuyenda. Iwe uyenera kundibereka pamsana<br />

kuti tikafike msanga.”<br />

Fisi anaberekadi Kalulu. Posakhalitsa onse anafika.<br />

Koma atafika pafupi ndi akazi aja Kalulu anauka<br />

n’kuimirira, ndipo anatenga ndodo yake amvekere,<br />

thya! kukwapula a Fisi. “Yenda bulu wanga! Tiye chita<br />

liwiro! Yenda bulu wangaa!” Kenako anayamba kuuza<br />

mbeta zija kuti, “Suja ndidakuuzani madona kuti fisi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

323


ndi bulu wanga!”<br />

Fisi atamva mawu amenewa anangolira, “Uwi!<br />

Uuuuuuuuuuuuuwi! Kalulu ndizo udakonza<br />

zimenezo, tenga akaziwo zako ziyende!” Atatero<br />

anangoti patchire lowu, zii! wapita. Akazi aja anati,<br />

“Zoonadi, a Kalulu samanamayi!” Ndiyeno Kalulu<br />

anati, “Paja ndinakuuzani kuti fisi ndi bulu wanga!<br />

Mwazionera nokhatu!”<br />

Kalulu anakwatira akazi aja, Mtimaukanena ndi<br />

Khumbo. Fisi ndi Kalulu anadana koopsa. Pakati<br />

pawo panali chidani chosamwerana madzi kuopa<br />

kuthirirana mankhwala.<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi n’chifukwa chiyani akazi awiri amene<br />

atchulidwa m’nkhaniyi ankafuna kukwatiwa ndi<br />

nyama zakuthengo?<br />

2. Kodi ndi ndani amene anakanidwa mochititsa<br />

manyazi?<br />

3. Nanga atsikanawa anavomera ndani?<br />

4. Kodi Kalulu anachita chiyani pofuna kulanda<br />

akaziwo?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

324


Kuunika ndi Mdima<br />

Tsiku lina Kuunika ndi Mdima kunayamba<br />

kukangana kuti adziwe amene anali wofunika<br />

kwambiri pakati pawo. Kuunika kunayamba<br />

kuyankhula modzigomera kumvekere, “Eee, ndine<br />

patali, zinthu zonse zimasangalala ndikamawala ndipo<br />

ndine wamphamvu zedi kuposa aliyense. Nditangoti<br />

ndisawale kwa masiku angapo zomera zonse zikhoza<br />

kufa. Anthu akhoza kumavala zovala zaziwisi komanso<br />

kumangopunthwa akamayenda. Kodi anthu otsogola<br />

ndi tekinoloje akanalowera kuti kukapala mphamvu<br />

zoti aunikire midzi yawo. Kunena zoona palibe amene<br />

angafikepo pamene ndinafika ine! Sindili ngati inuyo a<br />

mdima. Kuda muli bii ngati makala, moti umadziwa<br />

zoti pali munthu akatsokomola. Anthu alibe nawe<br />

ntchito, n’chifukwa chake amapala moto kwa ine<br />

n’kumaunikira usiku.” Mdima utamva chipongwe<br />

chimenechi unapsa mtima ndipo unauza Kuwala kuti,<br />

“Pakadapanda ine anthu sakanamaliza mkonono,<br />

bwenzi anthu akumwalira ndi tulo. Akuba sakadapata<br />

chawo chuma komanso Afisi akadavutika koopsa<br />

chifukwa cha njala, nanga adakamatola bwanji<br />

zowola. Iwe kuwala ndiwe woyerekedwa. Kodi sudziwa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

325


kuti anthu amadana nawe? Amati umawawaula,<br />

kuwaononga maso komanso kuwayambitsira<br />

matenda. Amakupherera ndi mwafuli, kuvala mandala<br />

komanso ena amakana kuyenda iwe ukamawala.<br />

Zikanakhala kuti ali ndi mphamvu zokuchotsa<br />

paudindo bwenzi atakuchotsa kalekale chifukwa<br />

anatopa nawe.” Kenako mkanganowo unafika povuta<br />

moti mdima unati, “Tiyeko tipandane tione uyo ali<br />

wadzitho komanso wofunika!” “Chabwino bwera<br />

ndikuphofomole uone,” anatero Kuunika. “Iwe<br />

Kuunika, undipeze madzulo kuti ndidzakuchotse<br />

chimbenene! Panopa ndikufuna ndithandize anthu<br />

kuti apeze ufulu wochita zomwe akufuna.<br />

Umawaphera anthu ufulu iwe! Udzamangidwatu,<br />

zoona ungamayalutse anthu olemekezeka!”<br />

“Chabwino, ndibwera!”<br />

Madzulo, Mdima unadikira mpaka kutopa, koma<br />

kuwala sikunatulukire. Unkangoyang’anira kunjira<br />

maso ali psuu! Tsiku lotsatira Kuwala nakonso<br />

kunadikira mpaka madzulo moti nakonso maso<br />

anafiiriratu psuu, koma sunaone mnzake akubwera.<br />

Usiku unayamba kudzitama umvekere, “Amati atani<br />

Kuunika kapolo? Akuchita mantha kuopa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

326


kupandidwa!” Masana nakonso Kuunika kunayamba<br />

kudzitama kumvekere, “Amati achite chiyani kapolo<br />

amene uja Mdima, wandiopatu!”<br />

Tsiku lina atakumana, ndewu inayamba masanasana.<br />

Nthawi ya madzulo, Kuunika kunagonja n’kugwera<br />

pansi kwalaaa! Mdima utaona zimenezi unati,<br />

“Heheeeedeee! Umati uchite chiyani kamwana iwee!”<br />

Pakati pa usiku, ndewu inabadwa, nthawi ya m’mawa<br />

usiku unagonja. Nakonso kuunika kunayamba<br />

kuseka, “Pwitipwitipwiti! Umati uchite chiyani mwana<br />

woonekera matumbo iwee! Pamenepa mpamene<br />

panayambira udani wawo. Kuunika kunadziwa kuti<br />

mwamuna mnzako mpachulu. Mdima nawonso<br />

unaona kuti mnzakeyo mpachulunso, moti mdima<br />

unkati ukaona kuwala akubwera poteropo, unkachoka<br />

n’kupita kwina. Nakonso kuunika kukaona kuti<br />

Mdima ukubwera, kunkasintha njira kapena<br />

kubwerera kwawo kukagona.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

327


Mafunso:<br />

1. Kodi pakati pa kuunika ndi mdima, chofunika<br />

kwambiri ndi chiyani?<br />

2. Kodi ndi pati pamene panayambira udani wa<br />

kuunika ndi kuwala?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

328


Nzeru za Kalulu<br />

M’nkhalango yotchedwa Ngwangwa m’dziko la Fukuto,<br />

munali nyama zosiyanasiyana. Chaka china mvula<br />

inakanika kugwa moti madzi ankasowa. Mkati mwa<br />

m’nkhalango ya Ngwangwa munali chitsime chimodzi<br />

chokha. Mwachidule tingati chitsimechi chimadziwika<br />

ndi dzina loti Mzizime. Chinali chitsime chamadzi<br />

okoma, ozizira bwino komanso ochotsa chipemba.<br />

Nyama zonse zinkapita kuchitsimechi kukamwa<br />

madzi. Nthawi zina zinkapezeka kuti chitsimechi<br />

chaphwa. Pofufuza, nyama zonse zinatsimikiza kuti<br />

anyani ndi amene ankaphwetsa chitsimecho chifukwa<br />

ankamwa madzi moipa kwambiri. Zitatero, Njovu<br />

inaitanitsa nyama zonse kuti zidzamve malamulo a<br />

chitsime cha Mzizime. “Ndati ndinene pano kuti<br />

anyani asiye kumwa nawo madzi a pachitsime<br />

chathuchi. Ndamva zoti anyaniwa ndi amene<br />

akumaliza madzi pachitsimechi. Choncho kuyambira<br />

lero, muonetsetse kuti anyani asamabwere kuno<br />

kudzamwa madzi! Nkhani imene ndinakuitanirani ndi<br />

imeneyi.”<br />

Njovu inapitiriza kunena kuti, “Iwe Mvuwu, Mbidzi,<br />

Mkango, Kadyamsonga ndi Nyamalikiti, imwani<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

329


madziwa tsopano tizipita. Koma muonetsetse kuti<br />

nyani asadzaoneke pachitsimechi. Amene adzagwire<br />

mbala zikuba madziwa, ndithu adzalandira mphoto<br />

yaikulu. Ine sindisamala za ufumu wanga ayi. Amene<br />

adzagwire mbala ikuba madziwa adzapatsidwa ufumu<br />

wangawu.”<br />

Kalulu anaimirira n’kunena kuti, “Ine mfumu ndili ndi<br />

njira yogwirira mbala imeneyi. Mundipatse nthawi.<br />

Mawa nyama zonse zisabwere kuchitsime kuno.<br />

Nyama zonse zibwere mkuja, mawa zitsotse osamwa<br />

madzi. Mkuja, nyama zonse zidzapeza mbala imene<br />

ikuba madzi a mu Mzizime. Nonse mudzabwere<br />

kudzaona mbalayo.” Nyama zonse zitamva mawu a<br />

Kalulu, zinakondwera ndipo nkhawa zawo zinayamba<br />

kuchepa.<br />

Kalulu atachoka apo, anatenga nkhwangwa n’kulowa<br />

m’tchire. Atatero, anapeza mtengo ndipo anasema<br />

chifanizo cha munthu. Anatenganso phula la njuchi<br />

ndi ulimbo n’kuyamba kumata thupi lonse la chosema<br />

chija. Atatha, anachinyamula n’kupita nacho<br />

pachitsime chija. Atafika, anatenga chifanizirocho<br />

n’kuchikumbira pansi kuti chiime chilili ngati<br />

munthu.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

330


Atamaliza kuchita zimenezi, Kalulu anapita kwa<br />

bwenzi lake Nyani ndipo anamuuza kuti, “Bwenzi<br />

langa, kodi dzulo unali kuti?” Nyani anayankkha kuti,<br />

“Bwanawe, ine dzulo pamodzi ndi banja langali,<br />

tinakaba madzi kuchitsime china pafupi pomwepa. Ife<br />

satiloleza kumwa madzi kumeneko chifukwa timati<br />

tikapita, chitsime chonse timachiphwetsa. Moti<br />

anatiletsa kuti tisadzamwenso madzi pachitsimecho.”<br />

Kalulu anauza Nyani kuti, “Bwenzi langa, ine<br />

ndabwera kudzakuchenjeza. Nyama zonse zaika<br />

mlonda kuchitsime chija. Mlondayo amafa msanga<br />

akamumenya kumsana kwake. Iwe mawa upite ndi<br />

banja lako kukamwa madzi. Ukasamale kuti mlondayo<br />

asakakupenye. Ndiye ukatulukire kumbuyo kwake<br />

ndipo usakaponde masamba ouma kuti mlondayo<br />

asakamve mtswatswa wako. Ukakafika kalimbe<br />

mtima, ukalikutumule khofi n’kumenya mlondayo,<br />

ukaona kuti nthawi yomweyo akafa. Uvutikirenji ndi<br />

ludzu ngati umachita kufuna kuti uzimwa madzi<br />

ambiri, si ndi mmene unabadwira! Ukakachipanda<br />

khofi, ukachipondenso ndi mwendo mwamphamvu,<br />

ukaona kuti nthawi yomweyo chafa ndipo iwe ukamwa<br />

madzi mtima uli zii.”<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

331


Nyani atamva izi anati, “Zikomo bwenzi langa. Wachita<br />

bwino kundipangira nzeru yotereyi, nanga tife ndi<br />

ludzu chitsime chilipo?” M’mawa kwambiri Nyani<br />

pamodzi ndi banja lake analawirira kuchitsime chija.<br />

Atafika pafupi nyani anabanika nalo khofi.<br />

Anatambasula dzanja lamanja ndipo analikutumula<br />

khofi, limvekere m’mutu mwa mlonda uja kuti phwaa!<br />

Pamene nyani ankati achotse dzanja, zachosoni,<br />

linakanirira. Analiponyanso lamanzere khofi kuti<br />

phwaa! Zachisoni linakaniriranso. Tsopano<br />

anamuponda mlonda ndi miyendo yonse iwiri,<br />

zachisoni, miyendo yonse inakanirira. Tsopano nyani<br />

anayankhula, “Aaaa! Koma iwe uli ndi chipongwe eti?<br />

Bwanji ukugwira dzanja langa? Tandisiya msanga!<br />

Ndati undisiye iweee! Kodi sukumvaaaaaaa? Eeee?”<br />

Nthawi yomweyo kunamveka kulira kwa nyama,<br />

nyamazo zimabwera kuchitsimeko kudzamwa madzi!<br />

Kalulu anali m’gulu la nyamazi. Kalulu anati, “A<br />

Njovu, taonani mbala ija iyoooo! yagwidwa. Ine<br />

ndangochepa msinkhu koma taonani mmene<br />

ndagwirira kapolo wanuyooo!” Nyama zonse<br />

zinathamanga, n’kugwira wakubayo. Posakhalitsa,<br />

Njovu inaveka Kalulu ufumu ndipo inati, “Ufumu ndi<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

332


wako chifukwa cha nzeru zako!”<br />

Mafunso:<br />

1. N’chifukwa chiyani Njovu inaitanitsa<br />

msonkhano?<br />

2. Kodi anyani analakwa chiyani kuti awakanize<br />

kumwa madzi a pachitsime chija?<br />

3. Nanga n’chifukwa chiyani Kalulu anapusitsa<br />

Nyani?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

333


Phwando la Kalulu ndi Fulu<br />

Kalekalelo, Kalulu ankakonda kutchera misampha.<br />

Nthawi zambiri iye ankati akagwira nyama,<br />

ankagawirako bwenzi la pamtima Fulu. Ankachita<br />

zimenezi akamachoka kowonjola nyama zomwe<br />

zinakodwa m’misampha yake.<br />

Pa nthawiyo, Njovu ndi Mvuwu zinali paubwenzi<br />

wobwerekana nsalu. Kumene kunali Njovu, a Mvuwu<br />

ankapezekanso komweko. Kangapo konse a Ng’ona<br />

anauzapo onsewa kuti, “Koma anzanga inu, ubwenzi<br />

wotere n’ngoipa. Bwanji simumafuna kutayana? Kodi<br />

simudziwa kuti mukadzakumana ndi ngozi mudzafera<br />

pamodzi?” “Hahaha! Mwana iwe ukuti chiyani?<br />

Akuluakulu ngati ife chingationekere n’chiyani?<br />

Sukudziwa kuti ife ndife mphangala zokhazokha?”<br />

anatero Njovu poyankha a Ng’ona. “Kodi mwana iwe,<br />

aliponso wina woposa ife pa mphamvu? Sudziwa eti?”<br />

Anafunsa chotero a Mvuwu.<br />

Tsiku lina Kalulu akuyendera misampha yake, anaona<br />

mapazi a Njovu ndi Mvuwu. Mumtima mwake ali,<br />

“Agalu amenewa tsiku lina tidzaonana. Amenewa ndi<br />

amene akumaba nyama m’misampha yanga, mbala<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

334


zakuba!”<br />

Kalulu atabwerera anafika kwa Fulu ali, “Bwenzi langa<br />

pepa, lerotu udyera therere. Mbala zikungoba nyama<br />

zanga m’misampha. Ndikukhulupirira kuti ndi Njovu<br />

ndi Mvuwu, ndaonera mapazi awo. Ndikadakhala ndi<br />

chingwe cholimba ndikadawatchera msampha,<br />

ndikanawaonetsa malodza.” Fulu anati, “Bwenzi langa,<br />

khala chete, ine ndili ndi chingwe chachitali cha<br />

nsambo zopota. Dikira ndikupatse. Ife tikufuna<br />

kumadya nyama tsiku ndi tsiku ndiye sitingalole agalu<br />

amenewa aziba nyama zako ayi.”<br />

M’mawa mwake, Kalulu anatenga chingwe chija<br />

n’kupita nacho pampita wa Njovu ndi Mvuwu.<br />

Atasunzumira potero, anaona Njovu ndi Mvuwu<br />

zikubwera. Kalulu anatenga chingwecho nachinjatirira<br />

ku muzu wa mtengo waukulu umene udatemedwa<br />

ndipo nayenso anachita ngati wadzinjata.<br />

Njovu ndi Mvuwu zitafika zinati, “Oooooooo! watani<br />

mnzathu woyenda?” Kalulu ali “Heeee!<br />

Sindingakuuzeni chifukwa sindifuna kuti anthu ena<br />

akumane ndi zimene ndikukumana nazo ine pano<br />

chifukwa tingachuluke. Komabe poti tonsefe ndife a<br />

mliyenda m’tchire muno, inu nokha ndikuuzani. Koma<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

335


mulonjeze kuti simuuza wina ayi!” “Kodi ife umatiyesa<br />

ana eti? Suona mathunthuwa kodi? Tatiuza,<br />

sitikanena kwa aliyense!” anatero Njovu.<br />

Tsopano Kalulu anati, “Monga mwaonera kuti chingwe<br />

chansambo za mkuwa simunachione, chingwe<br />

chimenechi chimapatsa mphamvu, kapena kuti<br />

mangolomera. Mwakuti inu nonsenu kuyambira lero<br />

simungandichite kanthu ayi, mwachepa!” “Aaaaaaa!<br />

Ukuti chiyani?” anafunsa Mvuwu.<br />

“Kodi simukumva? Inu nonsenu pa mphamvu, osati<br />

msinkhu ayi, mwachepa ndipo ndinu makanda<br />

ang’onoang’ono osamera ndi mano omwe! Kapena<br />

ndinene kuti ndinu nthumbidwa!” anatero Kalulu.<br />

Kalulu anapitiriza kunena kuti, “Ngati mukuchita<br />

makani, mawa tiyesane. Inu awiri mugwire chingwe<br />

cha nsambochi mukhale kuseri kwa kaphiri aka, ine<br />

ndikakhala kuseri kwa Phiri ilo. Nonsenu pamodzi<br />

mukakoke chingwechi kuti muone zimene zichitike.”<br />

Njovu inati, “Ha! Ndikangokusiyira Mvuwuyu basi,<br />

akathane nawe. Mwana wakhanda ungachite chiyani<br />

ndi mapiri ngati ano? Taona, kunotu ndi kugomo osati<br />

masewera ukuchita apawa.” Anatero a Njovu<br />

podzitamandira.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

336


M’mawa kutacha, onse anakumana pa kaphiri<br />

kotchedwa Talala. Chingwe cha mkuwa chija<br />

chinayalidwa kuseri ndi kuseri kwa phirilo. Fulu<br />

patsiku limeneli anabwera kudzawonerera<br />

mpikisanowo ndiponso anasankhidwa kukhala<br />

wolamulira mpikisanowo. Kalulu anatenga chingwe<br />

chija nachinjatirira kumtengo waukulu wa mlambe.<br />

Tsopano poyamba, a Njovu anasiyira a Mvuwu okha<br />

kuti akokane ndi Kalulu.<br />

Fulu analamulira motere, “Tsopano aliyense agwire<br />

chingwe! Konzekani, kokaaaaaaa!” Zimene zinaoneka<br />

pamenepo zinali zoopsa. Mvuwu idayesa kuchita<br />

kakalakakala koma inaona kuti Kalulu ali nju! “Pepa<br />

mnzanga Njovu. Nkhondo yakula, Kalulu ujadi ali ndi<br />

mphamvu.” Anayesanso ndithu ndi mphamvu zake<br />

zonse koma Kalulu anali nju! osasunthika. Kenako<br />

Mvuwu inati, “Achimwene a Njovu, tiyeni tithandizane!<br />

Mmenemo Fulu ali, “Koka! Kokaaa!” Pamenepo n’kuti<br />

mbali imene kunali Njovu ndi Mvuwu, mitengo<br />

itawandikawandika, ina itathyokeratu, miyala<br />

inkangogubuduzikagubuduzika, fumbi lili kobooo!<br />

Nthawi imeneyi, Kalulu n’kuti atangokhala pamwala<br />

ali neng’a, akusuta fodya ali phee. A Njovu anayesetsa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

337


kukoka koma kenaka anayamba kumangodzigwera<br />

okhaokha, kenaka kumangogwerana ndi a Mvuwu,<br />

Njovu itaona kuti zavuta inati, “Aaa! Koma n’zoonadi<br />

Kalulu lero kutichititsa manyazi chotere! Mnzanga<br />

Mvuwu, tiyeko tigonje timunyengerere kuti nafenso<br />

atigawireko mphamvu zakezo!”<br />

Tsopano Njovu ndi Mvuwu anakweza manja awo<br />

m’mwamba kusonyeza kugonja. Fulu analamula,<br />

“Chingwe pansi! Yagonja Njovu ndi Mvuwu! Kalulu<br />

wapambanaaa!” Nthawi yomweyo Kalulu anamasula<br />

chingwe chija n’kuchitaya pansi. Onse tsopano<br />

anakwera pamwamba pa phiri la Talala ndipo<br />

atakumana, a Njovu anati, “Aaa! Iwe Kalulu<br />

takhulupirira zija umanenazi. Tsopano madodafe<br />

ndithu tikhale opanda mphamvu? Ayi usatero,<br />

utipatseko mphamvu zakozi!” Kalulu anati, “Tiyeni<br />

nthawi yomwe ino pamalo pompaja kuti<br />

ndikakunjateni. Inu a Njovu tinjata chitamba<br />

chanuchi. Inu a Mvuwu tikunjatani miyendo yanuyi.”<br />

Atatha kuwanjata, Kalulu anawatembenukira<br />

amvekere: “Mwafa lero mafana! Mwafa lero! Mbala inu<br />

mwakhala mukundibera nyama zanga!” Njovu inati,<br />

“Hiii! Tikufa!” Mvuwunso ili, “Mayooo! Tikufa!” Ndiyetu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

338


panali matatalazi. Tsoka ilonso anali atatopa kale<br />

chifukwa cha mpikisano uja. Ndiyetu a Njovu<br />

amvekere khuu! kugwa, nawonso a Mvuwu, khuu!<br />

Kugwa chagada!<br />

Nthawi yomweyo Kalulu anathamanga kukasokolotsa<br />

ana ake amene anawabisa, mpeni uli kumanja ali,<br />

“Lero kuli chiphwando cha nyama yokhayokha.” Fulu<br />

naye ali, “Ine ndiyambira kuchekako Njovuyi. Lero kuli<br />

chiphwando chosasunsa.” Kalulu ndi ana ake pamodzi<br />

ndi Fulu anapanga chiphwando chadzaoneni ndipo<br />

anadya a Njovu ndi a Mvuwu.<br />

Mafunso<br />

1. Kodi ndi ndani ankaba nyama za Kalulu?<br />

2. Kodi chingwe cha mkuwa chinapatsadi<br />

mphamvu Kalulu?<br />

3. N’chifukwa chiyani Njovu ndi Mvuwu<br />

zinagonja?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

339


Chimene Kalulu Amagonera Diso Lili<br />

Tong’o!<br />

Tsiku lina Kalulu akuongola miyendo m’malunje<br />

anamva phokoso la nyama zomwe zinkaoneka kuti<br />

zinali pa chimsonkhano m’nkhalango yotchedwa<br />

Thuma. Pamene Kalulu anaima, anamva dzina lake<br />

likutamulidwa. Iye anadabwa popeza sanalandire<br />

mthenga wa msonkhano wotere. Kenaka anamva<br />

mawu onena za kuuma kwa mitengo ndi udzu. Chaka<br />

chimenecho mvula inapenga moti kunja kudali gwa<br />

chifukwa cha chilala. Udzu, mitengo komanso zomera<br />

zonse zinaumiratu. Chakudya cha nyama zonse<br />

chinkasowa moti m’masiku amenewo nyama<br />

zinkangodya dothi la mdambo. Nyamazi zinkatchula<br />

malo angati amenewa kuti Phukuto.<br />

Kalulu anayamba kupenekera kuti cholinga cha<br />

msonkhanowo chinali kukambirana za njala imene<br />

inali m’kamwam’kamwa. Kalulu anasendera pafupi<br />

ndithu ndipo anadabwa atangoona nyama<br />

zowerengeka zokha, popeza zinali pobisalika. Mawu a<br />

Njovu anali kumveka kuti, “Anzanga nonse mwabwera<br />

pano, njala ndimeneyi. Njala yopanda pothawira yotere<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

340


timaitcha chinkukuluzi. Koma ife bwanji kamwana<br />

kaja kamati ndi mfumuka palibe? Ka Kalulu<br />

kameneka ine ndimati ufumu wake uthe lero. Bwanji<br />

sabwera pamavuto ngati awa? Ine ndinam’tumira<br />

mthenga, koma onani sanabwere. N’chifukwa chaketu<br />

ine ndikuti ufumu wake watha lero! Nanga inu<br />

mukuganiza bwanji?” “Indeee! Tiyeni tipungure ufumu<br />

wakewo kuti aone polekera,” nyama zonse zinatero<br />

mwa mabvume.<br />

Zonse ankanena Njovu zoti adatuma mthenga kwa<br />

Kalulu, linali bodza lofuka utsi. Njovu inachita izi<br />

potengera chidani chakale. Inachita dala kuti Kalulu<br />

atsike pampando. Kenako kunatulukira chimoto<br />

chimene anthu a liwamba anatentha, ndipo Kalulu<br />

ataona motowo zinamuvuta popeza motowo<br />

unkalunjika pamene iye anabisala.<br />

Kalulu nzeru zinamuthera popeza amafuna kumva<br />

zonse zimene ankambirana makamaka zothetsa<br />

ufumu wake wa zaka zambiri m’nkhalangomo. Kalulu<br />

anangothawira kunyumba kwake kuti akayambe<br />

wapeza nzeru zina.<br />

Mmawa kutacha Kalulu anatuma mthenga kwa<br />

bwenzi lake Nyani, kuti awonjezere nzeru chifukwa<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

341


mumtima adati, “Nzeru umati n’za mnzako si za<br />

wekha. Mutu umodzi susenza tsindwi. Safunsa adadya<br />

phula. Nzeru zayekha adaviika nsima padziwe. Nyama<br />

ya liuma inafa ndi ludzu. Dombolo n’kuwombolana.<br />

Ndiye ine ndiyenera kufunsira nzeru kwa bwenzi<br />

langa.”<br />

Nyani asanafike, Kalulu anaika mphika pamoto<br />

kuphika zikhawo zosakaniza ndi bowa, chifukwa<br />

mkazi ake anali akudwala. “Odii! Odii kumeneko!”<br />

Mawu anamveka. “Lowani,” anatero Kalulu. “Oooo!<br />

Kodi ndi bwenzi langa Nyani! Khala pachitsapa.<br />

Pepatu wandipeza ndikuphika. Alamu ako sakupeza<br />

bwino ayi. Chibayo chidangowati thi! Moti ali<br />

dathidathi! Ndiye n’chifukwa chaketu wandipeza<br />

ndikuphika,” anatero Kalulu. “Pepa mbale wanga!”<br />

anayankha motero Nyani.<br />

“Ndakuitana ndine bwenzi langa,” anayamba nkhani<br />

motero Kalulu. “Kodi kumsonkhano dzulo lija kunali<br />

zotani? Ine sadanditumire mthenga wondidziwitsa.”<br />

“Ehe! Kodi waiwala, pajatu ife awiri ndife odedwa,<br />

inenso sadandiitane. Ndidangomva akuti a Njovu<br />

akuchotserani ufumu. Koma usade nkhawa mawa<br />

ndibwera ndi mankhwala. Malo ako ano<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

342


ndidzakonzakonza moti mitengo yonseyi ikhala ya<br />

biriwiri! Udzu onse wawumawu ukhalanso uli<br />

biriwiriwiri! Nyama zonse, zidzakukhumbira kwambiri<br />

n’chifukwa chake nditadzaikemo chinjoka kuti<br />

chizidzaluma nyama zakuba n’kufera pomwepo. Mbali<br />

iyo, ndi mankhwala omwewo, tibowola kasupe wa<br />

madzi ozizira bwino.”<br />

Atamaliza kudya chakudya chawo, Nyani anatsanzika<br />

n’kunyamuka kumapita kwawo. M’mawa kutacha<br />

Nyani anabwera ndi mankhwala ake amene<br />

anawatchula dzina loti Nkhonkha. Atachita<br />

mankhwala aja, panatuluka chinsipu chobiriwira,<br />

mitengo ya zipatso, ndipo madzi anabowoledwa moti<br />

ankangoti popopo!<br />

Mbiri ya mudzi wa Kalulu inamveka ndipo nyama<br />

zambiri zinkabwera kudzaona zodabwitsa ndi<br />

zachilendozo.<br />

Njati: Odii a Kalulu! Tadzaona zozizwitsazi! Zatheka<br />

bwanji?<br />

Kalulu: Ngakhale munathetsa ufumu wanga, koma<br />

mukufa ndi njala!<br />

Njati: Ngati ndine! Ee! Ndi a Njovutu omwe<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

343


mukulimbirana nawo ufumuwo!<br />

Mbidzi: Pepa Kalulu ndimwe nawo madzi ndingafe ndi<br />

ludzu!<br />

Nyama zonse zimene zidakaona mudzi wa Kalulu<br />

zinayamba kunyoza mawu amene ananena a Njovu oti<br />

Kalulu ufumu uthe. Njovu atamva zimenezi anachita<br />

manyazi popeza sankalandiranso ngakhale moni kwa<br />

nyama iliyonse.<br />

Nyama zonse tsopano zinaona kuti Kalulu ngakhale<br />

ufumu unamuchokera, koma anali wosangalala<br />

popeza anali kumwa ndi kudya bwino. Mkango ndi<br />

Mvuwu onse anapangana kuti aitanitse msonkhano.<br />

Nyama zonse pamodzi ndi Njovu zinabwera<br />

kudzakambirana za mavuto awo. Potsiriza anaganiza<br />

kuti onse apite kwa Kalulu kukapepesa ndi kufunsira<br />

nzeru kuti dziko libwerere msipu wosilirika ndi<br />

mitengo yobiriwira pamodzi ndi madzi.<br />

Atafika kwa Kalulu, nyama zonse zinanena mavuto<br />

awo mwatsatanetsatane.<br />

Mkango: Bwana Kalulu, ife tabwera kuti<br />

tidzakupepeseni. Tinakulakwirani zedi. Chimunthu<br />

china chachikulu khutu, chidatilakwitsa. Inu ufumu<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

344


wanu udalipoooo!<br />

Nyama zonse: Eeee! Indediii! Zoonaaa!<br />

Mkango: Bwana Kalulu, ife ana anu tikomereni mtima<br />

potikonzera nkhalango yathuyi. Taonani madzi<br />

mulibe, msipu mulibe komanso mitengo yayiwisi<br />

mulibe.<br />

Kalulu: Dzikoli silikonzeka! Ngati mukufuna kuti<br />

likonzeke aliyense akaphe amake. Kenako mubwere<br />

kuno mukabwere ndi mitu yawo kuti tidzakonzere<br />

mankhwala! Zamvekaa?<br />

Nyama zonse: Indeeeee! Mawa ife tibwera nayo<br />

mituyo!<br />

Kalulu: Ine kuti ndipeze mukuzionazi ndinayamba<br />

ndapha mayi anga, n’chifukwa chake lero ndili<br />

pabwino!<br />

Nyama zonse zinabalalika kukapha amayi awo<br />

n’kuwadula mitu. Mitu ija isadabwere, Kalulu<br />

ananyamula mayi ake usiku n’kukawabisa mumtengo<br />

mbali ina ya tchire m’nkhalango ya Thuma.<br />

Tsopano m’mawa kutacha, nyama zonse zinabwera<br />

ndi mitu ija. Kalulu anaunjika mituyo n’kuika nkhuni<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

345


pamwamba pake ndipo anaitentha mpaka inasanduka<br />

phulusa lokhalokha. Kenako Kalulu anati, “Eyaaa!<br />

Ntchito yanga ndayamba tsopano, pitani kwanu.<br />

Mukhoza kumwa nawo madzi angawa, mukhozanso<br />

kudya msipuwu ndi chilichonse chimene mungakonde<br />

musanapite kwanu!” Nyama zija zinayamba<br />

kulimbirana makamaka zikhawo za dinde, chinkhwisi,<br />

ndekera, nthochi ndi zina zotero.”<br />

Patapita masiku atatu nyama zija zinabweranso<br />

kudzafunsa ngati panali mwayi uja adalonjeza Kalulu.<br />

Kalulu anangowauza kuti phulusa la mitu lija<br />

likugwira ntchito. Anawauzanso kuti, “Tsopano dzikoli<br />

lili pafupi kukonzeka. Koma phulusa la mitu ija<br />

lachepa. Mvula ndi madzi ndimakapempha kwa Azimu<br />

a m’nkhalango ino, ndiwo amene afuna phulusa lina,<br />

lijali lachepa. Tsopano Azimuwo akufuna phulusa lina<br />

la mitu ya atate anu. Motero katengeni mitu ya atate<br />

anu kuti tidzasakanize pamodzi. Zikatero posachedwa<br />

mudzalandira zonse. Dziko lino la Thuma<br />

sikudzakhalanso mavuto ngati amenewa.”<br />

Nyama zonse zinapita n’kukapha atate awo<br />

n’kubweretsa mitu yonse kwa Kalulu. Kalulu anaotcha<br />

mitu ija n’kutenga phulusa. Nyama zija zinapita<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

346


Kalulu ananyamula atate ake n’kukawabisa kumalo<br />

kuja anabisa mayi ake. Pamene amachoka kumeneko,<br />

nyama zina zinamuona ndipo zinadodoma popeza<br />

anatenga nsengwa zodyera chakudya.<br />

Kenaka patatha sabata, nyama zonse zija<br />

zinabweranso kwa Kalulu. Kalulu anati, “Zoona<br />

anzanga muli m’mavuto, koma ndinapita kuphanga<br />

kumene kukhala Azimu. Phulusa lija ndinapereka<br />

koma Azimuwo akuti phulusa lija lachepa m’pofunika<br />

kuwonjezera lina la ana anu oyamba, achisamba.<br />

Mukatero sabata lamawa mulandira mvula ndi zonse<br />

zimene mukufuna.”<br />

Nyama zija zitamva mawu amenewa zinayamba<br />

kukhumudwa mumtima, zambiri zinayamba<br />

kung’ung’udza zimvekere, “Anzathu, izitu tipwetekeka<br />

nazo. Kodi tikathanso mtundu umene madziwo<br />

tidzamwa ndi ndani? Taonani umo taphera anthumu!<br />

Zabodza, Kalulu akufuna tithane tokha. Kodi<br />

simunamudziwebe Kalulu? Akhozatu kukhala<br />

akuponya nkhondo ndi ife mobisalira ife osadziwa.<br />

Tiyeni tichenjere!”<br />

Mmawa, nyama zonse zinabwera ndi mitu ya ana awo<br />

achisamba. Kalulu anatenga mitu ija n’kuiotcha ndipo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

347


anatenga phulusa lija. Patapita masiku awiri, nyama<br />

zonse zinabwera. Kalulu anati, “Ine ndabwera<br />

posachedwa kwa Azimu kuja. Phulusa lija ndapereka,<br />

koma akuti pakufunika kuwonjezeranso lina kuti<br />

tsopano likwane bwino n’cholinga choti mvula ibwere<br />

yoopsa, yamkokomo wa madzi. Motero mawa mubwere<br />

ndi mitu ya zitsitsa misepa zanu. Mufulumire!”<br />

Nyama zonse tsopano zinadodoma, zina zinakwiya<br />

koopsa. Fulu, Nkhandwe ndi Fisi anasankhidwa kuti<br />

akhale maso a nyama zonse. Udindo umene anali<br />

nawo ndi kubisalira Kalulu kuti aone mayendedwe ake<br />

chifukwa zochita za Kalulu zinayamba kuwatayitsa<br />

mtima.<br />

Nyama zonse zikupita kwawo, Kalulu analowa<br />

m’nyumba natulukamo ndi phukusi la masamba a<br />

mtengo wa msuku. Waliutsa liwiro kulowera kutchire.<br />

Fisi, Nkhandwe ndi Fulu, analiutsanso lawo liwiro<br />

kumutsatira. Atakweza maso, anaona Kalulu wagwira<br />

chingwe ali kukwera mumtengo, Fulu anati, “Anzanga<br />

mukuona zimene Kalulu akuchita?”<br />

Fisi: Kodi Kaluluyu ndizo amachita?<br />

Nkhandwe: Kodi n’kukhala chiyani chimenechi?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

348


Fulu: Bwino wosakweza mawu angatimve.<br />

Pamene Kalulu anafika patsinde la mtengo, anayamba<br />

kuimba kanyimbo namati, “Mayi! Mayi! Tayire<br />

kachingwe! Mayi! Mayi! Tayire kachingwe!”<br />

Tsopono anangoona chingwe kuchokera m’mwamba<br />

kuti sololokuu! Pansi khwa! Kalulu gwi! Lendee!<br />

kukwera mumtengo. Kalulu atatsika anapita<br />

kunyumba. Fisi anapita patsinde la mtengo uja<br />

nayambanso kuyimba, “Mayi! Mayi! Tayire kachingwe!<br />

Mayi! Mayi! Tayire kachingwe!”<br />

Posakhalitsa anaona chingwe chija kuti, sololokuu!<br />

Pansi chimvekere khwa! Fisi gwi! Lendee! mpaka<br />

anakafika m’mwamba muja kalakatu! Pamene amayi<br />

ndi atate a Kalulu anaona chilombo Fisi, analira,<br />

“Mayo! Mayoo!” Fisi ali “Mwafa lero! Mwafa lero!”<br />

Zitatero, Fisi ndi Nkhandwe anadula mitu ya awiriwa<br />

ndipo anatsika n’kupita kumene kunali nyama zina<br />

zija.<br />

Atafika Fisi anati, “Anzathu, tachita ntchito imene<br />

munatipatsa. Onani mitu iwiri iyi. Kalulu anabisa<br />

amake ndi atate ake kutchire m’mwamba. Ife<br />

tinamulondola, n’kubisala. Posakhalitsa tinaona<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

349


chingwe chili kuchoka m’mwamba. Iye atagwira<br />

chingwecho taona wakwera m’mwamba muja. Atatsika<br />

ifenso tinayimba kanyimbo kakeko ndipo tinangoona<br />

chatsika chingwe, ifenso pogwira, taona takwera<br />

m’mwamba muja. Poti tione, taona ndi amake ndi<br />

atate a Kalulu. Atationa basitu kuyambapo kulira. Ife<br />

ii basi, takong’ontha onse!” Nyama zonse zitamva<br />

zimenezi zinati, “Mwagwira ntchitooooooooooo!<br />

Mwagwira ntchitoo!”<br />

Kalulu atamva za nkhaniyi anathawa n’kukamanga<br />

malo atsopano pachitsamba. Kufikira lero amagona<br />

pachitsamba pomwepo maso ali tuzuuu kuopa<br />

milandu imene anapalamula pouza anthu kuti<br />

akufuna mitu yoti apetulire mvula.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

350


Mafunso<br />

1. N’chifukwa chiyani Njovu inaganiza zothetsa<br />

ufumu wa Kalulu?<br />

2. Kodi Kalulu anamva bwanji za nkhaniyi?<br />

3. Kodi mukuganiza kuti Kalulu ankanena zoona<br />

pamene anauza anzakewo kuti akufuna mitu<br />

n’cholinga choti awabweretsere mvula?<br />

4. N’chifukwa chiyani Kalulu amagona diso lili<br />

tuzu?<br />

5. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

351


Mfumu ndi Nyemba Zophika<br />

Kalelo kunali mfumu ina yokalamba kwambiri.<br />

Mfumuyi inali ndi nkhawa kwambiri chifukwa inalibe<br />

mwana woti n’kulowa ufumu wake. Ndiye itaona kuti<br />

chaka chimenecho sigonera, inaganiza zosankha<br />

mwana m’modzi wa mu ufumu wake kuti akhale<br />

mwana wake wodzalowa ufumuwo. Atafufuza m’dziko<br />

lonse anapeza anyamata khumi omwe ankaoneka<br />

okongola komanso a khalidwe labwino. Koma popeza<br />

inkafuna mwana m’modzi yekha inawauza kuti,<br />

“Tsopano chatsala chinthu chimodzi choti muchite<br />

kuti ndipeze mnyamata amene atakhale mwana<br />

wanga.” Kenako anapereka kwa mnyamata aliyense<br />

nyemba imodziimodzi n’kuwauza kuti akaidzale<br />

kunyumba kwawo n’kuisamalira kwa milingu itatu.<br />

Mwana amene adzasamalire bwino mbewu yake<br />

adzatengedwa kukhala mwana wa mfumu!<br />

Anyamatawo atangomva zimenezi analiyatsa liwiro, wa<br />

kwawo kukadzala mbewu yawo. Koma mnyamata wina<br />

anadabwa kwambiri ataona kuti mbewu yake<br />

sikumera. Mnyamatayo anachita chilichonse kuti<br />

imere, koma palibe chinachitika. Anzake aja<br />

anayamba kumuuza kuti akangogula ina n’kuidzala<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

352


chifukwa akapanda kutero zimuvuta. Koma makolo a<br />

mwanayo anali oopa Mulungu moti anamuuza kuti<br />

asachite zimenezo.<br />

Kenako tsiku linafika loti apite kwa amfumu aja. Ana<br />

asanu ndi anayi anapezeka kuti mbewu zawo<br />

zinamera. Mfumuyo inayamba kufunsa<br />

m’modzim’modzi kuti, “Kodi mbewu zimene<br />

ndinakupatsani zinamera?” ndipo anyamata onse<br />

anayankha kuti “Inde mfumu yanga.” Kenako<br />

mfumuyo inagwedezera mutu n’kupitanso kwa wina<br />

mpaka inafika pa mnyamata yemwe nyemba yake<br />

sinamere uja. Mnyamatayo ankangonjenjemera ndi<br />

mantha. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi unaitani<br />

nyemba imene ndinakupatsa kuti ukadzale?” Iye<br />

anati, “Ndinaidzala n’kumaisamalira koma sinamere.”<br />

Mfumuyo inagwira mkono wa mnyamatayo n’kupita<br />

naye pamene panali mpando wachifumu n’kunena<br />

kuti, “Nonse ndinakupatsani nyemba zophika, ndiye<br />

zatheka bwanji kuti za enanu zimere? Nanga nyemba<br />

zophika zingamere ngati? Munthu amene ndimafuna<br />

kuti akhale mwana wanga komanso adzakhale mfumu<br />

ndimafuna akhale ndi khalidwe limeneli la kuona<br />

mtima ndipo ndi mwana uyu yekha amene wachita<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

353


wino. Enanu zipitani!”<br />

Mafunso:<br />

1. Kodi n’chifukwa chiyani nyemba ya mwana<br />

wina sinamere?<br />

2. Kodi mukuganiza kuti nyemba zimene<br />

anyamata ena asanu ndi anayi aja anadzala zinali<br />

zimene anapatsidwa ndi mfumu ija?<br />

3. N’chifukwa chiyani mwana amene mbewu yake<br />

sinamere uja anasankhidwa kukhala mwana wa<br />

amfumu?<br />

4. Kodi tikuphunzirapo chiyani?<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

354


Angongole<br />

Mayi: Kukabwera angongole aja, uwauze kuti<br />

ndachokapo.<br />

Nyamazawo: Ndiwauze kuti mwapita kuti?<br />

Mayi: Kwa Chinsapo.<br />

Kenako angongole anatulukira ndipo anayamba<br />

kuodira.<br />

Angongole: Odiiiiii. Odi kumenekooo!<br />

Nyamazawo: Eeeee.<br />

Angongole: Mayi ako ali kuti?<br />

Nyamazawo: Achokapo, apita kwa Chinsapo.<br />

Angongole: Abwerako nthawi yanji?<br />

Nyamazawo: Aaaa, dikikirani kaye ndikawafunse.<br />

Angongole: Ukawafunsa bwanji, mmesa wati apita<br />

kwa chinsapo?<br />

Nyamazawo: Ayi, ali m’nyumbamu.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

355


Fisi Anakana Mtsatsi<br />

Mlenje wina anathedwa nzeru ndi chilombo chimene<br />

chinkabwera pakhomo pake n’kumagwira ziweto zake<br />

usiku. Tsiku lina anaganiza zotchera msampha ndipo<br />

usiku umenewo anagona khutu lili panja kuti akamva<br />

chinachake adzuke.<br />

Usikuwo anayamba kumva phokoso. Asuzumire,<br />

anangoona kuti ndi fisi wakodwa pamsampha. Fisiyo<br />

ankayesayesa kuti achokepo. Mlenjeyo ataona izi<br />

anayamba kukuwa amvekere, “Fisi kunoooooooooo!<br />

Bwerani mudzandithandize kuli fisi kunoooooooo!”<br />

Anthu a m’nyumba zoyandikira anatulukadi ndipo<br />

anagwira fisiyo n’kumukwidzinga ndi zingwe. Kenako<br />

anayamba kumuimba mlandu.<br />

Munthu wina anati, “Nkhosa zanga zakhala zikusowa,<br />

ayenera ndi fisi yemweyu amene amandibera.”<br />

Winanso anati, “Ife ndiye mbuzi zathu wamaliza zonse<br />

kudya.”<br />

Panabweranso mayi wina ndipo anati, “Nkhuku zathu<br />

zonse wamaliza kukhwasula ameneyu!”<br />

Ndiyeno nkhalamba ina inati, “Nanenso dzulo<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

356


ndinayanika mtsatsi zanga pathandala, ayenera wadya<br />

ndi yemweyu chifukwa zawowa.”<br />

Fisiyo atamva mawu amenewa anati, “Agogo inuyo<br />

ndiye mukunama, bola zimene anena anzanu zija.<br />

Koma za mtsatsizi ndiye ndakukanirani. Inetu<br />

sindidya mtsatsi.”<br />

Phunziro: Fisi angakhale munthu amene akuimbidwa<br />

mlandu. Ngakhale munthu atakhale woipa kwambiri, si<br />

bwino kumangomunamizira zimene sanachite.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

357


Mlenje ndi Mkango<br />

Tsiku lina mlenje wina anapita kutchire kukasaka<br />

nyama ndi agalu ake. Atafika malo ena, agalu akewo<br />

anasokolotsa Sakhwi n’kumugwira, koma mlenjeyo<br />

anawaletsa agaluwo kuti amusiye ndipo Sakhwiyo<br />

anathawa n’kukabisala kuphanga.<br />

Kenako mlenjeyo anapitirizabe kusaka ndipo anafika<br />

pafupi ndi dziwe lina. Pamalowo panali ntchefu moti<br />

agalu ake aja anagwira imodzi n’kuipha. Pamenepo<br />

mlenjeyo anasangalala zedi podziwa kuti tsiku<br />

limenelo akadyera nyama. Koma kenako kunayamba<br />

chimvula choopsa moti mphenzi sizinkati zaomba pati.<br />

Ataona zimenezi anaganiza zolowa m’phanga lina<br />

ndipo atangolowamo anapezamo ana a mkango. Koma<br />

popeza kunali mvula yoopsa, sakanachitira mwina<br />

koma kulowabe m’phangalo. Atangolowa, mkango<br />

ujanso nawo unatulukira. Nawonso unasokoloka<br />

m’tchire chifukwa cha mvulayo. Utafika pakhomo pa<br />

phanga lake unazindikira kuti m’phanga lakelo<br />

mwalowa munthu ndi agalu ake. Mkangowo sunafikire<br />

kulowamo chifukwa unkafuna kuti uonetsetse<br />

bwinobwino ngati mlenjeyo analidi yekha mphangalo.<br />

Kenako unafunsa munthuyo kuti, “Kodi ndiwe ndani<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

358


ukupezeka m’phanga langa?”<br />

Munthuyo anayankha mwamatha zedi kuti, “Ndine<br />

munthu mfumu yanga.”<br />

Kenako Mkangowo unati, “Ndiye popeza ndakupeza<br />

m’phanga langa, utenge ntchefu waphayo uwapatse<br />

agalu akowo kuti adye. Kenako iweyo udye agaluwo.<br />

Ineyo ndidya iweyo!”<br />

Munthuyo atamva izi anachita mantha zedi moti<br />

anayamba kunjenjemera komanso kudzikodzera.<br />

Koma mlenjeyo sanadziwe kuti Sakhwi<br />

anamupulumutsa uja anabisala momwemo.<br />

Sakhwiyo anauza mlenjeyo kuti, “N’chifukwa chiyani<br />

mukuchita mantha? Mkangowutu wanena kuti<br />

mutenge ntchefuyi mupatse agaluwa adye, kenako<br />

inuyo mudye agaluwo, ndipo Mkangowo udya inuyo.<br />

Pamapeto pake, ineyo ndidya Mkango ndi ana akewa.”<br />

Mkangowo utangomva zimenezo unachita mantha<br />

kwambiri moti unathawa.<br />

Phunziro: Ndi bwino kumathandiza ena chifukwa<br />

nawenso zikadzakuvuta akhoza kudzakuthandiza.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

359


<strong>Bonwell</strong> <strong>Rodgers</strong><br />

M’bukuli muli nthano za ana. Nthano zina ndi<br />

zoti zinalembedwa ndi akatswiri akale kwambiri<br />

ndipo zinamasuliridwa n’kukonzedwa mwina<br />

ndi mwina, pomwe zina ndi za kwathu konkuno<br />

ku Malawi. Nthanozi ndi zazifupi koma<br />

zosangalatsa.<br />

<strong>Mpandamachokero</strong> <strong>Anthology</strong><br />

360<br />

This book is dedicated to my<br />

beloved brother, Brian. I love<br />

you little brother and am<br />

always <strong>by</strong> your side.<br />

If I could save time in a<br />

bottle, the first thing that I’d<br />

like to do is to save every day<br />

till eternity passes away, just<br />

to spend them with you.<br />

If I could make days last<br />

forever, if words could make<br />

wishes come true, I’d save<br />

every day like a treasure and<br />

then again, I would spend<br />

them with you—Jim Croce.

Hooray! Your file is uploaded and ready to be published.

Saved successfully!

Ooh no, something went wrong!