Create successful ePaper yourself
Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.
mpingo uliwonse ndi dziko lirilonse muli anthu amene amabwera<br />
pamodzi mwa mwambo ndi khalidwe ndipo kenako kupita njira<br />
zosiyana, kukhala moyo wawo mmene chiwakondweretsera iwo<br />
eni. Mwina amachimwa mwaufulu ndi dala kapena satero konse.<br />
Komabe sinyumba ayi chifukwa sakhala ngati banja, tsiku ndi<br />
tsiku, pamodzi.<br />
Ndi pamene miyala yonse ikakamirana pamodzi pokha,<br />
momatidwa ndi chikondi cha zichitochito ndi ndi kumangidwa<br />
ndi mamangidwe a Mulungu, pamene amasanduka malo<br />
amene iye akhonza kuwatcha nyumba. Ngakhale uli mwala<br />
wamoyo wabwino ndikuyesa kukhala moyo wachiyero, ndi<br />
iwebe mwala umodzi. Ngati utenga mwala umenewo nauyika<br />
panthaka, sudzakhalabe nyumba ya <strong>Yesu</strong>. Iye safuna miyala<br />
yapayokha yokhala munda chabe ayi. Ife tiyenera tidzipange<br />
tokha, ngakhalenso kuzikakamiza tokha, kukakamirana<br />
pamodzi ndi miyala ina. Tsiku lirilonse tiyenera kudzilamula<br />
tokha kukakamirana pamodzi ndi miyala ina, mumamangidwe<br />
a Mulungu a Nyumba --------------------- pamene “tiyimirira,<br />
tikhala pansi, pamene tiyenda mumseu” pamodzi. Kuchaya<br />
Malaya pamodzi, ndi kupita kumsika pamodzi. Pamene<br />
tigwira ntchito mminda, tiumba njerwa, tidula nkhuni, tikonza<br />
chakudyatiyeni tichite ichi pamodzi kuti ife tikhale banja<br />
limodzi mmalo mwa anthu ambiri kapena mabanja ambiri. Ndi<br />
muzochitika “zazing’ona” izi zamoyo wa tsiku ndi tsiku pamene<br />
tingalimbitse ndi kulumikidza chikhulupiriro, chiyembekezo<br />
ndi chikondi chathu pamodzi. Zochita izi zatsiku ndi tsiku,<br />
zokhalidwa pamodzi ngati Banja, ziri “mazenera a moyo”<br />
amene amalora ife kusambitsana wina ndi mnzake mmadzi<br />
a Mau, koposa.<br />
Cha “kukhala nawo” mu miyambo yachipembezo ndi<br />
mmayimbidwe ndi mmauthenga a munthu oyera. <strong>Yesu</strong> sakumanga<br />
chilichose koma mpingo.<br />
<strong>Yesu</strong> adanena kuti ngati mumveradi funiro langa, mudzakhala<br />
ndi mazana a atate, amai, abale ndi alongo—osati anzathu ayi,<br />
koma zana la abale a m’banja okondana kwambiri. Ichi ndicho<br />
chifunira cha Mulungu. Izi ndizo ziphunzitso za <strong>Yesu</strong> Khristu—<br />
kuti amanga nyumba yake ndi katundu omangira wabwino.<br />
Katundu oyipa Sali olandilidwa ngati safuna kusintha pakumva<br />
mau a <strong>Yesu</strong>.<br />
Kumanga Kuti Ikhale Ya Mphamvu,<br />
Kulimbika Mtima kuti Tisinthe<br />
Pakatha zaka khumi zokhala a Khristu, anthu ambiri<br />
amuzipembedzo zowongoleredwa ndi Akulu a mpingo zamaziko<br />
ongokhala nawo pakupembedza sakhala wolimba kuposa mmene<br />
adaliri mzaka zawo zoyamba. Ichi sichabwino ayi. Ngati mwana<br />
wathu wachaka chimodzi akula kufika zaka khumi koma ali<br />
opanda mphanvu kapena nzeru koposa mmene adaliri ali ndi<br />
chaka chimodzi, ichi chingakhale chokhumudwitsa. Ngati uli ndi<br />
mwana wa zaka khumi mubanja mwanu amene adali wofooka<br />
ngati mwana wachaka chimodzi—monga tate kapena mai, ichi<br />
chikhonza kuswa mtima wanu, kodi sichingatero?<br />
Kodi muganizapo bwanji za Atate wathu a kumwamba m’mene<br />
amamvera pamene anthu ake onse ayenera kukhala amphamvu<br />
ndi nzeru ndi “ozadzidwa ndi Mzimu Oyera ndi ozadzidwa ndi<br />
nzeru,” “ndinso oyenera kukhala aphunzitsi panthawi ngati ino”<br />
“osati makanda ayi,” ogwira ntchito ya Mulungu koma ambiri mw<br />
aife sitili amphamvu koposa makanda a chaka chimodzi? Izi ndi<br />
zoona padziko lapansi, ndipo zimaswa mtima wa Mulungu. Ife<br />
sitingayimbe nyimbo zambiri kapena “kulalika” maulaliki ambiri<br />
kuti tisinthe ichi, chifukwa ife sitimanga munjira ya Mulungu mu<br />
Nyumba yake ya Mulungu.<br />
Mulungu ali ndi mamangidwe a Nyumba yake akuti timangire<br />
kuti ntchimo likhonza kuwomboledwa ndi kuphwanyika. Njira ya<br />
Mulungu “yomangira mpingo” imaloreza ubale kuti uchiritsidwe<br />
ndiponso tchimo ndi zifooka zichotsedwe. Uwu ndiwo mtima<br />
wa Mulungu kwa anthu ake kuzungulira pa dziko lonse. Ife tifuna<br />
tikuwuzeni inu m’mene anthu abwino angafikire pamphamvu<br />
zakuthekera tsopano.<br />
16 17