15.03.2015 Views

PDF - Yesu Kristo

PDF - Yesu Kristo

PDF - Yesu Kristo

SHOW MORE
SHOW LESS

Create successful ePaper yourself

Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.

mpingo uliwonse ndi dziko lirilonse muli anthu amene amabwera<br />

pamodzi mwa mwambo ndi khalidwe ndipo kenako kupita njira<br />

zosiyana, kukhala moyo wawo mmene chiwakondweretsera iwo<br />

eni. Mwina amachimwa mwaufulu ndi dala kapena satero konse.<br />

Komabe sinyumba ayi chifukwa sakhala ngati banja, tsiku ndi<br />

tsiku, pamodzi.<br />

Ndi pamene miyala yonse ikakamirana pamodzi pokha,<br />

momatidwa ndi chikondi cha zichitochito ndi ndi kumangidwa<br />

ndi mamangidwe a Mulungu, pamene amasanduka malo<br />

amene iye akhonza kuwatcha nyumba. Ngakhale uli mwala<br />

wamoyo wabwino ndikuyesa kukhala moyo wachiyero, ndi<br />

iwebe mwala umodzi. Ngati utenga mwala umenewo nauyika<br />

panthaka, sudzakhalabe nyumba ya <strong>Yesu</strong>. Iye safuna miyala<br />

yapayokha yokhala munda chabe ayi. Ife tiyenera tidzipange<br />

tokha, ngakhalenso kuzikakamiza tokha, kukakamirana<br />

pamodzi ndi miyala ina. Tsiku lirilonse tiyenera kudzilamula<br />

tokha kukakamirana pamodzi ndi miyala ina, mumamangidwe<br />

a Mulungu a Nyumba --------------------- pamene “tiyimirira,<br />

tikhala pansi, pamene tiyenda mumseu” pamodzi. Kuchaya<br />

Malaya pamodzi, ndi kupita kumsika pamodzi. Pamene<br />

tigwira ntchito mminda, tiumba njerwa, tidula nkhuni, tikonza<br />

chakudyatiyeni tichite ichi pamodzi kuti ife tikhale banja<br />

limodzi mmalo mwa anthu ambiri kapena mabanja ambiri. Ndi<br />

muzochitika “zazing’ona” izi zamoyo wa tsiku ndi tsiku pamene<br />

tingalimbitse ndi kulumikidza chikhulupiriro, chiyembekezo<br />

ndi chikondi chathu pamodzi. Zochita izi zatsiku ndi tsiku,<br />

zokhalidwa pamodzi ngati Banja, ziri “mazenera a moyo”<br />

amene amalora ife kusambitsana wina ndi mnzake mmadzi<br />

a Mau, koposa.<br />

Cha “kukhala nawo” mu miyambo yachipembezo ndi<br />

mmayimbidwe ndi mmauthenga a munthu oyera. <strong>Yesu</strong> sakumanga<br />

chilichose koma mpingo.<br />

<strong>Yesu</strong> adanena kuti ngati mumveradi funiro langa, mudzakhala<br />

ndi mazana a atate, amai, abale ndi alongo—osati anzathu ayi,<br />

koma zana la abale a m’banja okondana kwambiri. Ichi ndicho<br />

chifunira cha Mulungu. Izi ndizo ziphunzitso za <strong>Yesu</strong> Khristu—<br />

kuti amanga nyumba yake ndi katundu omangira wabwino.<br />

Katundu oyipa Sali olandilidwa ngati safuna kusintha pakumva<br />

mau a <strong>Yesu</strong>.<br />

Kumanga Kuti Ikhale Ya Mphamvu,<br />

Kulimbika Mtima kuti Tisinthe<br />

Pakatha zaka khumi zokhala a Khristu, anthu ambiri<br />

amuzipembedzo zowongoleredwa ndi Akulu a mpingo zamaziko<br />

ongokhala nawo pakupembedza sakhala wolimba kuposa mmene<br />

adaliri mzaka zawo zoyamba. Ichi sichabwino ayi. Ngati mwana<br />

wathu wachaka chimodzi akula kufika zaka khumi koma ali<br />

opanda mphanvu kapena nzeru koposa mmene adaliri ali ndi<br />

chaka chimodzi, ichi chingakhale chokhumudwitsa. Ngati uli ndi<br />

mwana wa zaka khumi mubanja mwanu amene adali wofooka<br />

ngati mwana wachaka chimodzi—monga tate kapena mai, ichi<br />

chikhonza kuswa mtima wanu, kodi sichingatero?<br />

Kodi muganizapo bwanji za Atate wathu a kumwamba m’mene<br />

amamvera pamene anthu ake onse ayenera kukhala amphamvu<br />

ndi nzeru ndi “ozadzidwa ndi Mzimu Oyera ndi ozadzidwa ndi<br />

nzeru,” “ndinso oyenera kukhala aphunzitsi panthawi ngati ino”<br />

“osati makanda ayi,” ogwira ntchito ya Mulungu koma ambiri mw<br />

aife sitili amphamvu koposa makanda a chaka chimodzi? Izi ndi<br />

zoona padziko lapansi, ndipo zimaswa mtima wa Mulungu. Ife<br />

sitingayimbe nyimbo zambiri kapena “kulalika” maulaliki ambiri<br />

kuti tisinthe ichi, chifukwa ife sitimanga munjira ya Mulungu mu<br />

Nyumba yake ya Mulungu.<br />

Mulungu ali ndi mamangidwe a Nyumba yake akuti timangire<br />

kuti ntchimo likhonza kuwomboledwa ndi kuphwanyika. Njira ya<br />

Mulungu “yomangira mpingo” imaloreza ubale kuti uchiritsidwe<br />

ndiponso tchimo ndi zifooka zichotsedwe. Uwu ndiwo mtima<br />

wa Mulungu kwa anthu ake kuzungulira pa dziko lonse. Ife tifuna<br />

tikuwuzeni inu m’mene anthu abwino angafikire pamphamvu<br />

zakuthekera tsopano.<br />

16 17

Hooray! Your file is uploaded and ready to be published.

Saved successfully!

Ooh no, something went wrong!