FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:
FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:
FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:
You also want an ePaper? Increase the reach of your titles
YUMPU automatically turns print PDFs into web optimized ePapers that Google loves.
MWACHIDULE<br />
Chimangiriro ichi chikufufuza mwadongosolo chilangizo m'mipingo ya Konveshoni ya<br />
Babatist m'Malawi (BACOMA), ndikuona kufunikira kwache pakati pa mtundu wa<br />
Achewa. Mu mbiri ya chiKhristu, zaonetsa kuti poyambirira mipingo imakana ndi<br />
kutsutsana ndi miyambo ya makolo. Koma pang'ono ndi pang'ono, mipingo inayamba<br />
kubvomereza ndi kulandira za miyamboyo pokhazikitsa mwambo wa chiKhristu<br />
m'malo mwake. M'mipingo yathu ya Babatist, nkhani ya chilangizo ndi chinamwali<br />
yakhala bvuto leni leni kutchito ya ubusa ndi yofalitsa Uthenga wa Yesu. Izi zakhala<br />
tero chifukwa chakulephera kwa BACOMA kumvetsetsa ndi kutanthauzira chinamwali<br />
kuchokera m'Mau a Mulungu muchinenero cha anthu.<br />
Ndicholinga cha chimangiriro ichi kuthandiza BACOMA, komanso mipingo yonse mu<br />
Afrika, kuti ikhale yomasuka kuphunzira za chikhalidwe ndi miyambo ya anthu.<br />
Cholinga ndi kuti mipingo imvetsetse mozama ndikukhoza kutanthauzira mwambo uli<br />
wonse pakugwiritsa ntchito Mau a Mulungu.a muchinenero chawo. Chimangirirochi ndi<br />
chiyambi chakulimbikitsa BACOMA pandondomeko yakukambirana, kulingirira, ndi<br />
kuphunzitsa anthu ake zokhuzana ndi chikhalidwe ndi miyambo ya makolo poyang'ana<br />
matanthauzo ache m'Bukhu Lopatulika.<br />
Chitatha chigawo chamayambo mu chimangirirochi, chigawo chachiwiri chayang'ana<br />
mbiri, chikhalidwe, ndi zikhulupiriro za mtundu wa Achewa. Chigawo chachitatu<br />
chaonetsa kukhazikitsidwa kwa mipingo wa Babatist kuchokera kumbali ziwiri.<br />
Poyamba kuchokera ku moyo wachipembezo ndi chikhalidwe cha azungu aBabatist<br />
akuAmerika, amene anabweretsa Uthenga Wabwino ku Afirika. Mbali yachiwiri<br />
yayang'ana zinthu zingapo zimene zinapangisa aMalawi kulandira ndi kufalitsanso<br />
Uthengawo kwa aMalawi anzawo. Popeza chilangizo ndi gawo la chikhalidwe chathu,<br />
chigawo chachinayi chalongosola mwatsatane-tsatane mwambo wa chinamwali cha<br />
Achewa cha ndakula. Chigawo chachisanu chapereka mbiri ya chilangizo makamaka<br />
mu BACOMA. Chigawo chachisanu ndi chimodzi chalongosola ndi kufufuza m'mene<br />
chilangizo chikuyendera m'mipingo ya Babatist. Kafukufuku waonetsa kuti chilangizo<br />
sichikukwaniritsa zosowa zeni-zeni za anthu pakulingirira zolinga zimene chinamwali<br />
chimakwaniritsa kwa Achewa. Chomwecho chigawo chotsiriza chapereka malingiriro<br />
ndindomeko yofunika kuti BACOMA iyambe kukambirana, kulingirira, ndi kuphu<br />
nzitsa akhristu za m'mene Mau a Mulungu amatanthauzira miyambo yamakolo athu.<br />
Chitsanzo cha chinamwali cha Chikhristu chaperekedwa potsirizira pa chimangirirochi.<br />
IV