28.07.2013 Views

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

SHOW MORE
SHOW LESS

You also want an ePaper? Increase the reach of your titles

YUMPU automatically turns print PDFs into web optimized ePapers that Google loves.

MWACHIDULE<br />

Chimangiriro ichi chikufufuza mwadongosolo chilangizo m'mipingo ya Konveshoni ya<br />

Babatist m'Malawi (BACOMA), ndikuona kufunikira kwache pakati pa mtundu wa<br />

Achewa. Mu mbiri ya chiKhristu, zaonetsa kuti poyambirira mipingo imakana ndi<br />

kutsutsana ndi miyambo ya makolo. Koma pang'ono ndi pang'ono, mipingo inayamba<br />

kubvomereza ndi kulandira za miyamboyo pokhazikitsa mwambo wa chiKhristu<br />

m'malo mwake. M'mipingo yathu ya Babatist, nkhani ya chilangizo ndi chinamwali<br />

yakhala bvuto leni leni kutchito ya ubusa ndi yofalitsa Uthenga wa Yesu. Izi zakhala<br />

tero chifukwa chakulephera kwa BACOMA kumvetsetsa ndi kutanthauzira chinamwali<br />

kuchokera m'Mau a Mulungu muchinenero cha anthu.<br />

Ndicholinga cha chimangiriro ichi kuthandiza BACOMA, komanso mipingo yonse mu<br />

Afrika, kuti ikhale yomasuka kuphunzira za chikhalidwe ndi miyambo ya anthu.<br />

Cholinga ndi kuti mipingo imvetsetse mozama ndikukhoza kutanthauzira mwambo uli<br />

wonse pakugwiritsa ntchito Mau a Mulungu.a muchinenero chawo. Chimangirirochi ndi<br />

chiyambi chakulimbikitsa BACOMA pandondomeko yakukambirana, kulingirira, ndi<br />

kuphunzitsa anthu ake zokhuzana ndi chikhalidwe ndi miyambo ya makolo poyang'ana<br />

matanthauzo ache m'Bukhu Lopatulika.<br />

Chitatha chigawo chamayambo mu chimangirirochi, chigawo chachiwiri chayang'ana<br />

mbiri, chikhalidwe, ndi zikhulupiriro za mtundu wa Achewa. Chigawo chachitatu<br />

chaonetsa kukhazikitsidwa kwa mipingo wa Babatist kuchokera kumbali ziwiri.<br />

Poyamba kuchokera ku moyo wachipembezo ndi chikhalidwe cha azungu aBabatist<br />

akuAmerika, amene anabweretsa Uthenga Wabwino ku Afirika. Mbali yachiwiri<br />

yayang'ana zinthu zingapo zimene zinapangisa aMalawi kulandira ndi kufalitsanso<br />

Uthengawo kwa aMalawi anzawo. Popeza chilangizo ndi gawo la chikhalidwe chathu,<br />

chigawo chachinayi chalongosola mwatsatane-tsatane mwambo wa chinamwali cha<br />

Achewa cha ndakula. Chigawo chachisanu chapereka mbiri ya chilangizo makamaka<br />

mu BACOMA. Chigawo chachisanu ndi chimodzi chalongosola ndi kufufuza m'mene<br />

chilangizo chikuyendera m'mipingo ya Babatist. Kafukufuku waonetsa kuti chilangizo<br />

sichikukwaniritsa zosowa zeni-zeni za anthu pakulingirira zolinga zimene chinamwali<br />

chimakwaniritsa kwa Achewa. Chomwecho chigawo chotsiriza chapereka malingiriro<br />

ndindomeko yofunika kuti BACOMA iyambe kukambirana, kulingirira, ndi kuphu­<br />

nzitsa akhristu za m'mene Mau a Mulungu amatanthauzira miyambo yamakolo athu.<br />

Chitsanzo cha chinamwali cha Chikhristu chaperekedwa potsirizira pa chimangirirochi.<br />

IV

Hooray! Your file is uploaded and ready to be published.

Saved successfully!

Ooh no, something went wrong!