28.07.2013 Views

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

SHOW MORE
SHOW LESS

Create successful ePaper yourself

Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.

Anamkungwi amuonetse mtsikana kabvalidwe ka mwele bwino-bwino. Amupatse nayenso<br />

achite monga waonera mpakana akhonze ndipo anthu alulutire. Amuonetsenso kachapidwe<br />

ndi kasungidwe kache pamene nyimbo ikuimbidwabe. Potsiriza abwereze kumulongosolela<br />

kuti:<br />

While still singing, the instructresses should demonstrate and teach her well how to wear the menses linen and<br />

how to clean and take care ofthem. They should then explain the following to her:<br />

Tsopanotu iye ayenera kudzisamalira thupi lake koposa kale. Akhale waukhondo nthawi<br />

zonse ndi thupi ndi zobvala zake. Mtsikana adzisamalire kwenikweni thupi lake ndi nsaru<br />

zake panthawi imene ali mumsambo kuti asapezeke akutulutsa fungo loipa. Komanso<br />

asakhetsere paliponse mwazi wamsambo, popeza zimachititsa manyazi kuti ena aone mwazi<br />

umenewu. Kuyimba kupitirire.<br />

Now she must take care ofher body more than before. She needs to keep her body and her clothes clean at all<br />

times, particularly when she is menstruating so that no bad smell comes out. She needs to make sure that no<br />

blood stains remain anywhere for is it a shameful thing for people to see the stains. The singing continues.<br />

12. Kumana, kumana mtsikana x 2<br />

Mmati undipatse<br />

Wabvundikira<br />

13. Mulungu adawauza Adamu nda aHava<br />

Muberekane, muchurukane<br />

Refuse, refuse the girl<br />

I wanted you to give me<br />

You have covered<br />

God told Adam and Eve<br />

Be fruitful, and increase in number<br />

Longosolani kuti njira imene amatipatsira ana Mulungu ndi yakugonana mwamuna ndi<br />

mkazi amene ali pabanja. Kugonana kwa mwamuna ndi mkazi amene sali pabanja ndi<br />

chimo la chigololo pamaso pa Mulungu ('Usachite chigololo' Eksodo 20:14; 1 Akorinto<br />

6:13, 19).<br />

Explain that God gives us children through sexual activity in a marriage. Therefore sex outside marriage is<br />

adultery to God ('Do not commit adultery' Exodus 20:14; 1 Corinthians 6:13,19).<br />

14. Kodi lamulo la Mulungu likuti chiani?<br />

Likuti Usachite chigololo<br />

Thupiri si/ili la chigololo<br />

15. Kodi abale simudziwa eel<br />

Simudziwaaa eel<br />

Kodi abale simudziwa eel<br />

Simudziwaa eel<br />

Thupi lanu liri kachisi, liri kachisi<br />

Wa Mzimu Woyeraaa!<br />

What does God's law say?<br />

It says do not commit adultery<br />

The body is not for adultery<br />

Friends, do you not know eh!<br />

Do you not know eh!<br />

Friends, do you not know eh!<br />

Do you not know eh!<br />

Your body is a temple, is a temple<br />

Ofthe Holy Spiritiii!<br />

Onse azibvina akugwira thupi lao ndikusonyeza kumwamba kokhala Mzimu Woyera.<br />

They should be dancing while touching their bodies and pointing towards heaven where the Holy Spirit is.<br />

16. Mwendo, mwendo nkuyendera<br />

Maso, maso nkupenyera<br />

Chimodzimodzi, ziwalo zachinsinsi<br />

Ntchito yake m 'banja<br />

Leg, leg is for walking<br />

Eyes, eyes are for looking<br />

Similarly, private parts<br />

Their job is in marriage<br />

209

Hooray! Your file is uploaded and ready to be published.

Saved successfully!

Ooh no, something went wrong!