FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:
FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:
FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:
Create successful ePaper yourself
Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.
Anamkungwi amuonetse mtsikana kabvalidwe ka mwele bwino-bwino. Amupatse nayenso<br />
achite monga waonera mpakana akhonze ndipo anthu alulutire. Amuonetsenso kachapidwe<br />
ndi kasungidwe kache pamene nyimbo ikuimbidwabe. Potsiriza abwereze kumulongosolela<br />
kuti:<br />
While still singing, the instructresses should demonstrate and teach her well how to wear the menses linen and<br />
how to clean and take care ofthem. They should then explain the following to her:<br />
Tsopanotu iye ayenera kudzisamalira thupi lake koposa kale. Akhale waukhondo nthawi<br />
zonse ndi thupi ndi zobvala zake. Mtsikana adzisamalire kwenikweni thupi lake ndi nsaru<br />
zake panthawi imene ali mumsambo kuti asapezeke akutulutsa fungo loipa. Komanso<br />
asakhetsere paliponse mwazi wamsambo, popeza zimachititsa manyazi kuti ena aone mwazi<br />
umenewu. Kuyimba kupitirire.<br />
Now she must take care ofher body more than before. She needs to keep her body and her clothes clean at all<br />
times, particularly when she is menstruating so that no bad smell comes out. She needs to make sure that no<br />
blood stains remain anywhere for is it a shameful thing for people to see the stains. The singing continues.<br />
12. Kumana, kumana mtsikana x 2<br />
Mmati undipatse<br />
Wabvundikira<br />
13. Mulungu adawauza Adamu nda aHava<br />
Muberekane, muchurukane<br />
Refuse, refuse the girl<br />
I wanted you to give me<br />
You have covered<br />
God told Adam and Eve<br />
Be fruitful, and increase in number<br />
Longosolani kuti njira imene amatipatsira ana Mulungu ndi yakugonana mwamuna ndi<br />
mkazi amene ali pabanja. Kugonana kwa mwamuna ndi mkazi amene sali pabanja ndi<br />
chimo la chigololo pamaso pa Mulungu ('Usachite chigololo' Eksodo 20:14; 1 Akorinto<br />
6:13, 19).<br />
Explain that God gives us children through sexual activity in a marriage. Therefore sex outside marriage is<br />
adultery to God ('Do not commit adultery' Exodus 20:14; 1 Corinthians 6:13,19).<br />
14. Kodi lamulo la Mulungu likuti chiani?<br />
Likuti Usachite chigololo<br />
Thupiri si/ili la chigololo<br />
15. Kodi abale simudziwa eel<br />
Simudziwaaa eel<br />
Kodi abale simudziwa eel<br />
Simudziwaa eel<br />
Thupi lanu liri kachisi, liri kachisi<br />
Wa Mzimu Woyeraaa!<br />
What does God's law say?<br />
It says do not commit adultery<br />
The body is not for adultery<br />
Friends, do you not know eh!<br />
Do you not know eh!<br />
Friends, do you not know eh!<br />
Do you not know eh!<br />
Your body is a temple, is a temple<br />
Ofthe Holy Spiritiii!<br />
Onse azibvina akugwira thupi lao ndikusonyeza kumwamba kokhala Mzimu Woyera.<br />
They should be dancing while touching their bodies and pointing towards heaven where the Holy Spirit is.<br />
16. Mwendo, mwendo nkuyendera<br />
Maso, maso nkupenyera<br />
Chimodzimodzi, ziwalo zachinsinsi<br />
Ntchito yake m 'banja<br />
Leg, leg is for walking<br />
Eyes, eyes are for looking<br />
Similarly, private parts<br />
Their job is in marriage<br />
209