28.07.2013 Views

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

FROM CHINAMWALI TO CHILANGIZO:

SHOW MORE
SHOW LESS

Create successful ePaper yourself

Turn your PDF publications into a flip-book with our unique Google optimized e-Paper software.

for a while from norrnallife and put into seclusion to receive instruction or mwambo in order to live according<br />

to the accepted standards of the society. These ancestral customs are passed on from generation to generation<br />

through the chinamwali rite.<br />

Kuyambira kale Chikhristu chakhala chikufika kwa anthu amene akhazikika mumiyambo<br />

yamakolo awo. Ndipo pakuona kuti chinamwali ndichofunika kumitundu ya anthu ambiri,<br />

Akhristu adaona kuti ndikofunika kukonza zinamwali zachikhristu kuti zilowe m'malo mwa<br />

zamakolo. Kuno ku Malawi aKhristu adaika chilangizo mmalo mwa chinamwali. Ndiye<br />

kuti chilangizo ndi chiphunzitso cha chiKhristu chimene namwali amalandira pamene watha<br />

msinkhu, pakukwatiwa, mimba yoyamba ndi kubadwa kwa mwana. Koma mwambo weniweni<br />

womubvinira mtsikiana uchedwebe ndi dzina loti chinamwali. Alangizi (mlangizi,<br />

mmodzi) ndiwo adalowa mmalo mwa anamkungwi.<br />

Christianity has always come to a people who believe in the ancestral customs. Initiation is very important to<br />

many societies. It is therefore important for Christianity to take initiation very seriously. Here in Malawi<br />

chilangizo was introduced to take the place of chinamwali. Chilangizo is therefore a general term referring to<br />

the Christian instruction or teaching that is given to a girl upon her first menstruation, on marriage, during the<br />

first pregnancy, and the birth of the fust baby. Alangizi took the place of anamkungwi. However, the actual<br />

ceremony retains the term chinamwali. The instructresses are called alangizi (mlangizi, singular).<br />

Popeza anthu onse adalengedwa ndi Mulungu, muchifaniziro chake ndi mchikhalidwe chake<br />

(Genesis 1:26), ndiye kuti mwambo wa Mulungu ndi umene upatsa munthu khalidwe<br />

loyenera, osati makolo adafa kale. Uwu tiupeza rnBukhu lake Lopatulika.. Ndi chifukwa<br />

chake Chikhristu chiyenera kuphunzitsa anthu ache chikonzero cha Mulungu pa kutha<br />

msinkhu, ukwati, mimba, komanso kubereka ndi kulera mwana, kuti aliyense akhale monga<br />

Mulungu afunira. Mau a Mulungu akhale otisonyeza zoyenera, kuti anthu azimvera ndi<br />

kuchita zomwe Bible likubvomereza.<br />

Since all people were created by God, in his own image and in his likeness (Genesis 1:26), it is God's mwambo<br />

(instruction/teaching) that gives us true chikhalidwe (character). We fmd God's mwambo in his Holy Bible.<br />

That is why it is important for the Chritian tradition to teach its people God's purpose for puberty, marriage,<br />

pregnancy, child-birth, and upbringing. The Bible must therefore be the people's life map. They must obey<br />

only what the Bible affirms from their cultures.<br />

Ndi udindo wa mpingo uliwonse kuphunzitsa anthu ake mwambo wa Chikhristu kupyolera<br />

muzinamwali, popeza ndi njira imene mitundu yambiri imaphunzirira miyambo.<br />

It is the responsibility of every congregation to teach her members the Christian customs through chinamwali<br />

for that is the method through which many societies learn well.<br />

WOYENERA KULANGIZIDWA NDANI?<br />

WHO SHOULD BE COUNSELLED?<br />

Potsatira chinamwali chamakolo, ndikofuna kuti ulangizi wachiKhristu utsatirenso magawo<br />

onse a paumoyo wa munthu. Ndiye amene ayenera kulangizidwa ndi mwana, msungwana,<br />

komanso mayi. Ndiye ulangizi umene uli m'kabukhumu ndi wa msungwana asanathe<br />

msinkhu, pamene watha msinkhu, pamene wapeza bwenzi lokwatirana naye, ukwati wake,<br />

mimba yoyamba, kubadwa mwana woyamba, komanso wa amayi onse. Popeza imfa irinso<br />

ndi mwambo wake, Mpingo uyenera kukonza malangizo ndi ziphunzitso zosiyana-siyana<br />

zokhuzana ndi imfa.<br />

Following the traditional way, the Christian initiation should follow the person's life from birth to death. So a<br />

child, a girl, and a woman or mother should receive counsel. The instruction in this booklet therefore is for a<br />

girl before her puberty, upon her puberty, in courtship, at her marriage, at her first pregnancy, after the birth of<br />

200

Hooray! Your file is uploaded and ready to be published.

Saved successfully!

Ooh no, something went wrong!